Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

63 Mau a Mulungu Okhudza Kuchita Chifuniro Chake

Monga mwana wa Mulungu, ndili ndi mwayi waukulu wotsogozedwa ndi Atate wanga wakumwamba, amene ali ndi nzeru zonse ndi mphamvu zonse. Iye amadziwa njira iliyonse yomwe ndikuyenda ndipo akufunitsitsa kundionetsa njira yabwino yoti nditsatire.

Mu Masalmo 321, pali lonjezo lamphamvu: "Ndidzakulangiza, ndidzakusonyeza njira yoyenera kupitamo; ndidzakupatsa uphungu, maso anga adzakhala pa iwe." Ndikafunafuna chifuniro cha Mulungu pa chisankho chilichonse, sindingasochere. Ndikungofunika kuzindikira ndi kudzilola kutsogozedwa ndi Mzimu Woyera pa chisankho chilichonse, chifukwa Iye amadziwa chomwe chili chabwino kwa ine.

Kudalira Yesu kumatanthauza kupambana pa chilichonse chimene ndichita. Kumbukira kuti chifuniro cha Mulungu kwa ine n’chabwino, chokondweretsa, ndiponso changwiro, ngakhale ndisanayambe kuchita zinthu m’njira yanga. Lolani Ambuye alembe nkhani yatsopano kwa ine, kumene chilichonse chidzagwirizana ndi chifuniro Chake, kumene maganizo anga sadzakhala patsogolo, koma zomwe Mulungu akufuna kwa ine.


1 Atesalonika 5:18

M'zonse yamikani; pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu cha kwa inu, mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:17

Ndipo dziko lapansi lipita, ndi chilakolako chake; koma iye amene achita chifuniro cha Mulungu akhala kunthawi yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:1

Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu, mwa chifuniro cha Mulungu, kwa oyera mtima amene ali mu Efeso, ndi kwa iwo okhulupirika mwa Khristu Yesu:

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 143:10

Mundiphunzitse chokonda Inu; popeza Inu ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu ndi wokoma; munditsogolere kuchidikha.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:36

Pakuti chikusowani chipiriro, kuti pamene mwachita chifuniro cha Mulungu, mukalandire lonjezano.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:17

Chifukwa chake musakhale opusa, koma dziwitsani chifuniro cha Ambuye nchiyani.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:8

kuchita chikondwero chanu kundikonda, Mulungu wanga; ndipo malamulo anu ali m'kati mwamtima mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:10

Ufumu wanu udze. Kufuna kwanu kuchitidwe, monga Kumwamba chomwecho pansi pano.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 4:3

Pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu, chiyeretso chanu, kuti mudzipatule kudama;

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 7:17

Ngati munthu aliyense afuna kuchita chifuniro chake, adzazindikira za chiphunzitsocho, ngati chichokera kwa Mulungu, kapena ndilankhula zochokera kwa Ine ndekha.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:27

ndipo Iye amene asanthula m'mitima adziwa chimene achisamalira Mzimu, chifukwa apempherera oyera mtima monga mwa chifuniro cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 1:3-4

Chisomo kwa inu, ndi mtendere wa kwa Mulungu Atate, ndi Ambuye wathu Yesu Khristu,

amene anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu, kuti akatilanditse ife m'nyengo ya pansi pano ino yoipa, monga mwa chifuniro cha Mulungu ndi Atate wathu;

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 22:42

nati, Atate, mukafuna Inu, chotsani chikho ichi pa Ine; koma si kufuna kwanga ai, komatu kwanu kuchitike.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:6

si monga mwa ukapolo wa pamaso, monga okondweretsa anthu, komatu monga akapolo a Khristu, akuchita chifuniro cha Mulungu chochokera kumtima;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:17

Pakuti, kumva zowawa chifukwa cha kuchita zabwino, ndi kumva zowawa chifukwa cha kuchita zoipa, nkwabwino kumva zowawa chifukwa cha kuchita zabwino, ngati chitero chifuniro cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:19

Koteronso iwo akumva zowawa monga mwa chifuniro cha Mulungu aike moyo wao ndi kuchita zokoma m'manja a Wolenga wokhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 6:40

Pakuti chifuniro cha Atate wanga ndi ichi, kuti yense wakuyang'ana Mwana, ndi kukhulupirira Iye, akhale nao moyo wosatha; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomaliza.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 6:39

Koma chifuniro cha Iye amene anandituma Ine ndi ichi, kuti za ichi chonse Iye anandipatsa Ine ndisatayeko kanthu, koma ndichiukitse tsiku lomaliza.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:15

Pakuti chifuniro cha Mulungu chitere, kuti ndi kuchita zabwino mukatontholetse chipulukiro cha anthu opusa;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:2

Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuniro cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 9:31

Tidziwa kuti Mulungu samvera ochimwa. Koma ngati munthu aliyense akhala wopembedza Mulungu nachita chifuniro chake, amvera ameneyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 1:12-13

Koma onse amene anamlandira Iye, kwa iwo anapatsa mphamvu yakukhala ana a Mulungu, kwa iwotu, akukhulupirira dzina lake;

amene sanabadwe ndi mwazi, kapena ndi chifuniro cha thupi, kapena ndi chifuniro cha munthu, koma cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 18:14

Chomwecho sichili chifuniro cha Atate wanu wa Kumwamba kuti mmodzi wa ang'ono awa atayike.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:21

Si yense wakunena kwa Ine, Ambuye, Ambuye, adzalowa mu Ufumu wa Kumwamba; koma wakuchitayo chifuniro cha Atate wanga wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:16-17

Pakuti chilichonse cha m'dziko lapansi, chilakolako cha thupi ndi chilakolako cha maso, matamandidwe a moyo, sizichokera kwa Atate, koma kudziko lapansi.

Ndipo dziko lapansi lipita, ndi chilakolako chake; koma iye amene achita chifuniro cha Mulungu akhala kunthawi yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 3:35

Pakuti aliyense achita chifuniro cha Mulungu, yemweyo ndiye mbale wanga, ndi mlongo, ndi amai.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:20-21

Koma Mulungu wa mtendere amene anabwera naye wotuluka mwa akufa Mbusa wamkulu wa nkhosa ndi mwazi wa chipangano chosatha, ndiye Ambuye wathu Yesu,

akuyeseni inu opanda chilema m'chinthu chilichonse chabwino, kuti muchite chifuniro chake; ndi kuchita mwa ife chomkondweretsa pamaso pake, mwa Yesu Khristu; kwa Iyeyu ukhale ulemerero kunthawi za nthawi. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:21

Lemekezani Yehova, inu makamu ake onse; inu atumiki ake akuchita chomkondweretsa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 12:50

Pakuti aliyense amene adzachita chifuniro cha Atate wanga wa Kumwamba, yemweyo ndiye mbale wanga, ndi mlongo wanga, ndi amai wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 29:11

Pakuti ndidziwa malingiriro amene ndilingiririra inu, ati Yehova, malingiriro a mtendere, si a choipa, akukupatsani inu adzukulu ndi chiyembekezero.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:46

Ndipo munditchuliranji Ine, Ambuye, Ambuye, ndi kusachita zimene ndizinena?

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 6:38

Pakuti ndinatsika Kumwamba, si kuti ndichite chifuniro changa, koma chifuniro cha Iye amene anandituma Ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:13

pakuti wakuchita mwa inu kufuna ndi kuchita komwe, chifukwa cha kukoma mtima kwake, ndiye Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 4:34

Yesu ananena nao, Chakudya changa ndicho kuti ndichite chifuniro cha Iye amene anandituma Ine, ndi kutsiriza ntchito yake.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 1:10

Pakuti kodi ndikopa anthu tsopano, kapena Mulungu? Kapena kodi ndifuna kukondweretsa anthu? Ndikadakhala wokondweretsabe anthu, sindikadakhala kapolo wa Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 11:2

Ndipo anati kwa iwo, M'mene mupemphera nenani, Atate, Dzina lanu liyeretsedwa; Ufumu wanu udze;

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:39

Ndipo anamuka patsogolo pang'ono, nagwa nkhope yake pansi, napemphera, nati, Atate ngati nkutheka, chikho ichi chindipitirire Ine; koma si monga ndifuna Ine, koma Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:15

Mukadanena inu, Akalola Ambuye, ndipo tikakhala ndi moyo, tidzachita kakutikakuti.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:105

Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga, ndi kuunika kwa panjira panga.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 14:8

Pakuti tingakhale tili ndi moyo, tikhalira Ambuye moyo; kapena tikafa, tifera Ambuye; chifukwa chake tingakhale tili ndi moyo, kapena tikafa, tikhala ake a Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:4-5

Mundidziwitse njira zanu, Yehova; Mundiphunzitse mayendedwe anu.

Munditsogolere m'choonadi chanu, ndipo mundiphunzitse; pakuti Inu ndinu Mulungu wa chipulumutso changa; Inu ndikuyembekezerani tsiku lonseli.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 41:10

usaope, pakuti Ine ndili pamodzi ndi iwe; usaopsedwe, pakuti Ine ndine Mulungu wako; ndidzakulimbitsa; inde, ndidzakuthangata; inde, ndidzakuchirikiza ndi dzanja langa lamanja la chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:14

Muli abwenzi anga inu, ngati muzichita zimene ndikulamulani inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 1:4

amene anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu, kuti akatilanditse ife m'nyengo ya pansi pano ino yoipa, monga mwa chifuniro cha Mulungu ndi Atate wathu;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:16-18

Kondwerani nthawi zonse;

Pempherani kosaleka;

M'zonse yamikani; pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu cha kwa inu, mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:21

akuyeseni inu opanda chilema m'chinthu chilichonse chabwino, kuti muchite chifuniro chake; ndi kuchita mwa ife chomkondweretsa pamaso pake, mwa Yesu Khristu; kwa Iyeyu ukhale ulemerero kunthawi za nthawi. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako;

umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:10-11

Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse; ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.

Ndizindikira koposa okalamba popeza ndinasunga malangizo anu.

Ndinaletsa mapazi anga njira iliyonse yaoipa, kuti ndisamalire mau anu.

Sindinapatukane nao maweruzo anu; pakuti Inu munandiphunzitsa.

Mau anu azunadi powalawa ine! Koposa uchi m'kamwa mwanga.

Malangizo anu andizindikiritsa; chifukwa chake ndidana nao mayendedwe onse achinyengo.

Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga, ndi kuunika kwa panjira panga.

Ndinalumbira, ndipo ndinatsimikiza mtima, kuti ndidzasamalira maweruzo anu olungama.

Ndazunzika kwambiri: Ndipatseni moyo, Yehova, monga mwa mau anu.

Landirani, Yehova, zopereka zaufulu za pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni maweruzo anu.

Moyo wanga ukhala m'dzanja langa chikhalire; koma sindiiwala chilamulo chanu.

Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga, kuti ndisalakwire Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:28

Ndipo tidziwa kuti amene akonda Mulungu zinthu zonse zithandizana kuwachitira ubwino, ndiwo amene aitanidwa monga mwa kutsimikiza kwa mtima wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:4

Udzikondweretsenso mwa Yehova; ndipo Iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 10:31

Chifukwa chake mungakhale mudya, mungakhale mumwa, mungakhale muchita kanthu kena, chitani zonse ku ulemerero wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 5:9

Chifukwa chakenso tifunitsitsa, kapena kwathu kapena kwina, kukhala akumkondweretsa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:6

pokhulupirira pamenepo, kuti Iye amene anayamba mwa inu ntchito yabwino, adzaitsiriza kufikira tsiku la Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:2

Odala iwo akusunga mboni zake, akumfuna ndi mtima wonse;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:14-15

Ndipo uku ndi kulimbika mtima kumene tili nako kwa Iye, kuti ngati tipempha kanthu monga mwa chifuniro chake, atimvera;

ndipo ngati tidziwa kuti atimvera chilichonse tichipempha, tidziwa kuti tili nazo izi tazipempha kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:3

Pereka zochita zako kwa Yehova, ndipo zolingalira zako zidzakhazikika.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:30

Ndipo ndikudandaulirani, abale, ndi Ambuye wathu Yesu Khristu, ndi chikondi cha Mzimu, kuti mudzalimbike pamodzi ndi ine m'mapemphero anu kwa Mulungu chifukwa cha ine;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:27

Mundizindikiritse njira ya malangizo anu; kuti ndilingalire zodabwitsa zanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 2:10

Pakuti ife ndife chipango chake, olengedwa mwa Khristu Yesu, kuchita ntchito zabwino, zimene Mulungu anazipangiratu, kuti tikayende m'menemo.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:13

Pakuti adakuitanani inu, abale, mukhale mfulu; chokhacho musachite nao ufulu wanu chothandizira thupi, komatu mwachikondi chitiranani ukapolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:16

Chomwecho muwalitse inu kuunika kwanu pamaso pa anthu, kuti pakuona ntchito zanu zabwino, alemekeze Atate wanu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:23-24

chilichonse mukachichita, gwirani ntchito mochokera mumtima, monga kwa Ambuye, osati kwa anthu ai;

podziwa kuti mudzalandira kwa Ambuye mphotho ya cholowa; mutumikira Ambuye Khristu mwaukapolo.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga, dzina lanu ndi loyera ndi loopsa, palibe chofanana ndi kuyera kwanu! Ndikubwera kwa inu kudzera mwa Ambuye wathu Yesu Khristu, ndikupemphani kuti mundithandize kukhala mogwirizana ndi chifuniro chanu ndikupha ine mwini, kudzikuza kwanga, ndikutha kusiya zokondweretsa zanga ndikumvetsa kuti chifuniro chanu ndi chabwino, chokondweretsa ndi changwiro pa moyo wanga. Mawu anu amati: "Chifukwa chake, musakhale opusa, koma dziwani chifuniro cha Ambuye." Atate, m'nthawi yovutayi mundithandize kuzindikira poganiza zochita ndipo osadzakhala wopusa patsogolo pa dziko lino, koma kukhala ndi nzeru yochokera kumwamba kuti nditsogoleredwe ndi Mzimu wanu Woyera, chifukwa chitsimikizo chokha cha chipambano changa ndi kukhala paubwenzi wolimba ndi inu. Ambuye, ndikupemphani kuti musunge mtima wanga ndi kundiphunzitsa tsiku lililonse kuchita zomwe mukufuna ndikupanga zisankho zoyenera, chifukwa zimenezo zidzasonyeza chifuniro chanu ndipo zidzabweretsa madalitso pa moyo wanga. Tsatani ulendo wanga wa tsiku ndi tsiku, kuti ndimvetse tsiku lililonse kuti sizokhudza ine koma inu. M'dzina la Yesu, Ameni.