Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Aefeso 5:17 - Buku Lopatulika

17 Chifukwa chake musakhale opusa, koma dziwitsani chifuniro cha Ambuye nchiyani.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

17 Chifukwa chake musakhale opusa, koma dziwitsani chifuniro cha Ambuye nchiyani.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

17 Nchifukwa chake musakhale opusa, koma dziŵani zimene Ambuye afuna kuti muchite.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

17 Choncho musakhale opusa, koma mudziwe zimene Ambuye akufuna kuti muchite.

Onani mutuwo Koperani




Aefeso 5:17
17 Mawu Ofanana  

Koma kwa munthu anati, Taonani, kuopa Ambuye ndiko nzeru; ndi kupatukana nacho choipa ndiko luntha.


Kumuopa Yehova ndiko chiyambi cha nzeru; onse akuchita chotero ali nacho chidziwitso chokoma; chilemekezo chake chikhalitsa kosatha.


Mundizindikiritse njira ya malangizo anu; kuti ndilingalire zodabwitsa zanu.


Nzeru ya wochenjera ndiyo yakuti azindikire njira yake; koma utsiru wa opusa ndiwo chinyengo.


pompo udzazindikira kuopa Yehova ndi kumdziwadi Mulungu.


Gula ntheradi, osaigulitsa; nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.


Pakuti anthu anga apusa, sandidziwa Ine; ali ana opulukira sazindikira; ali ochenjera kuchita choipa koma kuchita chabwino sakudziwa.


Ngati munthu aliyense afuna kuchita chifuniro chake, adzazindikira za chiphunzitsocho, ngati chichokera kwa Mulungu, kapena ndilankhula zochokera kwa Ine ndekha.


Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuniro cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.


Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru;


Chifukwa chake asungeni, achiteni; pakuti ichi ndi nzeru zanu ndi chidziwitso chanu pamaso pa mitundu ya anthu akumva malemba ndi kuti, Ndithu mtundu waukulu uwu, ndiwo athu anzeru ndi akuzindikira.


Mwa ichi ifenso, kuyambira tsiku limene tidamva, sitileka kupembedzera ndi kupempherera inu, kuti mukadzazidwe ndi chizindikiritso cha chifuniro chake mu nzeru zonse ndi chidziwitso cha mzimu,


Muyendere munzeru ndi iwo akunja, kuchita machawi nthawi ingatayike.


M'zonse yamikani; pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu cha kwa inu, mwa Khristu Yesu.


kuti nthawi yotsalira simukakhalenso ndi moyo m'thupi kutsata zilakolako za anthu, koma chifuniro cha Mulungu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa