Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 15:14 - Buku Lopatulika

14 Muli abwenzi anga inu, ngati muzichita zimene ndikulamulani inu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

14 Muli abwenzi anga inu, ngati muzichita zimene ndikulamulani inu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

14 Inu ndinu abwenzi anga ngati muchita zimene ndikulamulani.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

14 Inu ndinu abwenzi anga ngati muchita zimene Ine ndikulamulani.

Onani mutuwo Koperani




Yohane 15:14
19 Mawu Ofanana  

ndi Azariya mwana wa Natani anayang'anira akapitao, ndipo Zabudi mwana wa Natani anali wansembe ndi nduna yopangira mfumu,


Pakuti anaumirira Yehova osapatuka pambuyo pake, koma anasunga malamulo amene Yehova adawalamulira Mose.


Sindinu Mulungu wathu, amene munainga nzika za m'dziko muno pamaso pa ana anu Israele, ndi kulininkha kwa mbeu ya Abrahamu bwenzi lanu kosatha?


Ndipo Mose ndi Aroni anachita monga Yehova anawalamulira, momwemo anachita.


Woyanjana ndi ambiri angodziononga; koma lilipo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.


Ndalowa m'munda mwanga, mlongo wanga, mkwatibwi: Ndatchera mure wanga ndi zonunkhiritsa zanga; ndadya uchi wanga ndi chisa chake; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Idyani, atsamwalinu, imwani, mwetsani chikondi.


Koma iwe, Israele, mtumiki wanga, Yakobo, amene ndinakusankha, mbeu ya Abrahamu bwenzi langa;


ndipo analowa, nakhalamo; koma sanamvere mau anu, sanayende m'chilamulo chanu; sanachite kanthu ka zonse zimene munawauza achite; chifukwa chake mwafikitsa pa iwo choipa chonsechi;


Ndipo ndinachita monga momwe anandilamulira, ndinatulutsa akatundu anga usana, ngati a pa ulendo wa kundende, ndi madzulo ndinaboola pakhoma ndi dzanja langa, ndinawatulutsa pali mdima, ndi kuwasenza paphewa panga pamaso pao.


Pakuti aliyense amene adzachita chifuniro cha Atate wanga wa Kumwamba, yemweyo ndiye mbale wanga, ndi mlongo wanga, ndi amai wanga.


Ndipo ndinena kwa inu, abwenzi anga, Musaope iwo akupha thupi, ndipo akatha ichi alibe kanthu kena angathe kuchita.


Ngati mudziwa izi, odala inu ngati muzichita.


Ngati mukonda Ine, sungani malamulo anga.


Iye wakukhala nao malamulo anga, ndi kuwasunga, iyeyu ndiye wondikonda Ine; koma wondikonda Ine adzakondedwa ndi Atate wanga, ndipo Ine ndidzamkonda, ndipo ndidzadzionetsa ndekha kwa iye.


Mwamva kuti Ine ndinanena kwa inu, Ndimuka, ndipo ndidza kwa inu. Mukadandikonda Ine, mukadakondwera kuti ndipita kwa Atate; pakuti Atate ali wamkulu ndi Ine.


Amake ananena kwa atumiki, Chimene chilichonse akanena kwa inu, chitani.


ndipo anakwaniridwa malembo onenawa, Ndipo Abrahamu anakhulupirira Mulungu, ndipo kudawerengedwa kwa iye chilungamo; ndipo anatchedwa bwenzi la Mulungu.


Pakuti ichi ndi chikondi cha Mulungu, kuti tisunge malamulo ake: ndipo malamulo ake sali olemetsa.


Pamenepo anatsikira popunthirapo, nachita zonse monga umo mpongozi wake adamuuza.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa