Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Luka 6:46 - Buku Lopatulika

46 Ndipo munditchuliranji Ine, Ambuye, Ambuye, ndi kusachita zimene ndizinena?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

46 Ndipo munditchuliranji Ine, Ambuye, Ambuye, ndi kusachita zimene ndizinena?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

46 “Bwanji mumangoti, ‘Ambuye, Ambuye,’ koma chonsecho simuchita zimene ndimanena?

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

46 “Kodi nʼchifukwa chiyani munditchula kuti, ‘Ambuye, Ambuye’ koma simuchita zimene Ine ndinena?

Onani mutuwo Koperani




Luka 6:46
9 Mawu Ofanana  

Mwana alemekeza atate wake, ndi mnyamata mbuye wake; ngati Ine tsono ndine atate, uli kuti ulemu wanga? Ngati Ine ndine mbuye, kundiopa kuli kuti? Ati Yehova wa makamu kwa inu ansembe akupeputsa dzina langa. Ndipo mukuti, Tapeputsa dzina lanu motani?


Koma pambuyo pake anadzanso anamwali enawo, nati, Mbuye, mbuye, mutitsegulire ife.


Ndipo uyonso amene analandira talente imodzi, anadza, nati, Mbuye, ndinakudziwani inu kuti ndinu munthu wouma mtima, wakututa kumene simunafese, ndi wakusonkhanitsa kumene simunawaze;


Pomwepo iwonso adzayankha kuti, Ambuye, tinakuonani liti wanjala, kapena waludzu, kapena mlendo, kapena wamaliseche, kapena m'nyumba yandende, ndipo ife sitinakutumikirani Inu?


Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti chimene munthu achifesa, chimenenso adzachituta.


Khalani akuchita mau, osati akumva okha, ndi kudzinyenga nokha.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa