Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

63 Mauthenga a Mulungu Okhudza Ufulu Wachisankho

Munthu aliyense ali ndi udindo pa zochita zake. Mulungu sakukakamiza chifuniro chake pa ife ayi, nthawi zonse amatipatsa njira ziwiri: yabwino ndi yoipa, temberero kapena dalitso, moyo kapena imfa, ndipo ndife amene timasankha. Chilichonse chimene timachita pa moyo wathu, timachita ndi chifukwa, kaya zisankho zathu zikhale zabwino kapena zoipa.

Ufulu wosankha uwu ndi mphatso yochokera kwa Mulungu, ndipo pa izi, Mulungu sali nawo mphamvu, chifukwa munthu aliyense amasankha chomwe akuona kuti ndi choyenera. Zina timazichita chifukwa cha chilakolako champhamvu, pamene zina timazichita popanda kudziwa kuti tikufunadi kuchita zimenezo.

Apa ndiye pali mfundo ya ufulu wosankha: kusankha mogwirizana ndi zomwe tikufuna. Ufulu wosankha umenewu umatibweretsera pa mikhalidwe iwiri yauzimu: "kupulumuka kapena kutayika" (Yohane 3:36). "Wokhulupirira Mwana ali nawo moyo wosatha; koma wosakhulupirira Mwana sadzaona moyo, koma mkwiyo wa Mulungu ukhala pa iye.”


Masalimo 119:30

Ndinasankha njira yokhulupirika; ndinaika maweruzo anu pamaso panga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:173

Dzanja lanu likhale lakundithandiza; popeza ndinasankha malangizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:31

Usachitire nsanje munthu wachiwawa; usasankhe njira yake iliyonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:12

Munthuyo wakuopa Yehova ndani? Adzamlangiza iye njira adzasankheyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:13

Pakuti adakuitanani inu, abale, mukhale mfulu; chokhacho musachite nao ufulu wanu chothandizira thupi, komatu mwachikondi chitiranani ukapolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 54:6

Ine mwini ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu, ndidzayamika dzina lanu, Yehova, pakuti nlokoma.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 9:17

Pakuti ngati ndichita ichi chivomerere, mphotho ndili nayo; koma ngati si chivomerere, anandikhulupirira mu udindo.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 30:19

Ndichititsa mboni lero, kumwamba ndi dziko lapansi zitsutse inu; ndaika pamaso panu moyo ndi imfa, mdalitso ndi temberero; potero, sankhani moyo, kuti mukhale ndi moyo, inu ndi mbeu zanu;

Mutu    |  Mabaibulo
Oweruza 10:14

Mukani ndi kufuulira kwa milungu munaisankha, ikupulumutseni nyengo ya kusauka kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:13-15

Munthu poyesedwa, asanena, Ndiyesedwa ndi Mulungu; pakuti Mulungu sangathe kuyesedwa ndi zoipa, ndipo Iye mwini sayesa munthu:

koma munthu aliyense ayesedwa pamene chilakolako chake cha iye mwini chimkokera, ndikumnyenga.

Pamenepo chilakolakocho chitaima, chibala uchimo; ndipo uchimo, utakula msinkhu, ubala imfa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 7:17

Ngati munthu aliyense afuna kuchita chifuniro chake, adzazindikira za chiphunzitsocho, ngati chichokera kwa Mulungu, kapena ndilankhula zochokera kwa Ine ndekha.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 2:17

koma mtengo wakudziwitsa zabwino ndi zoipa usadye umenewo; chifukwa tsiku lomwe udzadya umenewo udzafa ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 3:6

Ndipo pamene anaona mkaziyo kuti mtengo unali wabwino kudya, ndi kuti unali wokoma m'maso, mtengo wolakalakika wopatsa nzeru, anatenga zipatso zake, nadya, napatsanso mwamuna wake amene anali naye, nadya iyenso.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:5

Ine ndine mpesa, inu ndinu nthambi zake: wakukhala mwa Ine, ndi Ine mwa iye, ameneyo abala chipatso chambiri; pakuti kopanda Ine simungathe kuchita kanthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:5-8

Pakuti iwo amene ali monga mwa thupi asamalira zinthu za thupi; koma iwo amene ali monga mwa mzimu, asamalira zinthu za mzimu:

pakuti chisamaliro cha thupi chili imfa; koma chisamaliro cha mzimu chili moyo ndi mtendere.

Chifukwa chisamaliro cha thupi chidana ndi Mulungu; pakuti sichigonja ku chilamulo cha Mulungu, pakuti sichikhoza kutero.

Ndipo iwo amene ali m'thupi sangathe kukondweretsa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yoswa 24:14-15

Ndipo tsopano, opani Yehova ndi kumtumikira ndi mtima wangwiro ndi woona; nimuchotse milungu imene makolo anu anaitumikira tsidya lija la mtsinje, ndi mu Ejipito; nimutumikire Yehova.

Ndipo ngati kutumikira Yehova kukuipirani mudzisankhire lero amene mudzamtumikira, kapena milungu imene anaitumikira makolo anu okhala tsidya lija la mtsinje, kapena milungu ya Aamori amene mukhala m'dziko lao; koma ine, ndi a m'nyumba yanga, tidzatumikira Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 2:16-17

Ndipo Yehova Mulungu anamuuza munthuyo, nati, Mitengo yonse ya m'munda udyeko;

koma mtengo wakudziwitsa zabwino ndi zoipa usadye umenewo; chifukwa tsiku lomwe udzadya umenewo udzafa ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yoswa 24:15

Ndipo ngati kutumikira Yehova kukuipirani mudzisankhire lero amene mudzamtumikira, kapena milungu imene anaitumikira makolo anu okhala tsidya lija la mtsinje, kapena milungu ya Aamori amene mukhala m'dziko lao; koma ine, ndi a m'nyumba yanga, tidzatumikira Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 56:4-5

Pakuti atero Yehova kwa mifule imene isunga masabata, nisankha zinthu zimene zindikondweretsa Ine, nigwira zolimba chipangano changa,

Kwa iyo ndidzapatsa m'nyumba yanga ndi m'kati mwa makoma anga malo, ndi dzina loposa la ana aamuna ndi aakazi; ndidzawapatsa dzina lachikhalire limene silidzadulidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 6:16

Kodi simudziwa kuti kwa iye amene mudzipereka eni nokha kukhala akapolo ake akumvera iye, mukhalatu akapolo ake a yemweyo mulikumvera iye; kapena a uchimo kulinga kuimfa, kapena a umvero kulinga kuchilungamo?

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:29

chifukwa anada nzeru, sanafune kuopa Yehova;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 10:23

Zinthu zonse ziloleka; koma sizipindula zonse. Zinthu zonse ziloleka; koma sizimanga zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 65:12

ndidzasankhiratu inu kulupanga, ndipo inu nonse mudzagwada ndi kuphedwa; pakuti pamene ndinaitana, inu simunayankhe; pamene ndinanena, simunamve; koma munachita choipa m'maso mwanga, ndi kusankha chimene Ine sindinakondwere nacho.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:9

Mtima wa munthu ulingalira njira yake; koma Yehova ayendetsa mapazi ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 14:12

Chotero munthu aliyense wa ife adzadziwerengera mlandu wake kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:2

Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuniro cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 6:12

Zinthu zonse ziloledwa kwa ine; koma si zonse zipindula. Zinthu zonse ziloledwa kwa ine, koma sindidzalamulidwa nacho chimodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 55:6-7

Funani Yehova popezeka Iye, itanani Iye pamene ali pafupi;

woipa asiye njira yake, ndi munthu wosalungama asiye maganizo ake, nabwere kwa Yehova; ndipo Yehova adzamchitira chifundo; ndi kwa Mulungu wathu, pakuti Iye adzakhululukira koposa.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 3:20

Taona, ndaima pakhomo, ndigogoda; wina akamva mau anga nakatsegula pakhomo, ndidzalowa kwa iye, ndipo ndidzadya naye, ndi iye ndi Ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:13-14

Lowani pa chipata chopapatiza; chifukwa chipata chili chachikulu, ndi njira yakumuka nayo kukuonongeka ili yotakata; ndipo ali ambiri amene alowa pa icho.

Pakuti chipata chili chopapatiza, ndi ichepetsa njirayo yakumuka nayo kumoyo, ndimo akuchipeza chimenecho ali owerengeka.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 8:34-36

Yesu anayankha iwo, nati, Indetu, indetu, ndinena kwa inu kuti yense wakuchita tchimo ali kapolo wa tchimolo.

Koma kapolo sakhala m'nyumba nthawi yonse; mwana ndiye akhala nthawi yonse.

Chifukwa chake ngati Mwana adzakuyesani inu aufulu, mudzakhala mfulu ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:5-6

Pakuti iwo amene ali monga mwa thupi asamalira zinthu za thupi; koma iwo amene ali monga mwa mzimu, asamalira zinthu za mzimu:

pakuti chisamaliro cha thupi chili imfa; koma chisamaliro cha mzimu chili moyo ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:15-17

Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru;

akuchita machawi, popeza masiku ali oipa.

Chifukwa chake musakhale opusa, koma dziwitsani chifuniro cha Ambuye nchiyani.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako;

umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:16

monga mfulu, koma osakhala nao ufulu monga chobisira choipa, koma ngati akapolo a Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 3:9

Ambuye sazengereza nalo lonjezano, monga ena achiyesa chizengerezo; komatu aleza mtima kwa inu, wosafuna kuti ena aonongeke, koma kuti onse afike kukulapa.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 11:26-28

Taonani, ndilikuika pamaso panu lero dalitso ndi temberero;

dalitso, ngati mudzamvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikuuzani lero lino;

koma temberero, ngati simudzamvera malamulo a Yehova Mulungu wanu, ndi kupatuka m'njira ndikuuzani lero lino, kutsata milungu ina imene simunaidziwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:21

Muli zolingalira zambiri m'mtima mwa munthu; koma uphungu wa Yehova ndiwo udzaimika.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:16-17

Pakuti chilichonse cha m'dziko lapansi, chilakolako cha thupi ndi chilakolako cha maso, matamandidwe a moyo, sizichokera kwa Atate, koma kudziko lapansi.

Ndipo dziko lapansi lipita, ndi chilakolako chake; koma iye amene achita chifuniro cha Mulungu akhala kunthawi yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 11:9

Kondwera ndi unyamata wako, mnyamata iwe; mtima wako nukasangalale masiku a unyamata wako, nuyende m'njira za mtima wako, ndi monga maso ako aona; koma dziwitsa kuti Mulungu adzanena nawe mlandu wa zonsezi.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:7-8

Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti chimene munthu achifesa, chimenenso adzachituta.

Pakuti wakufesera kwa thupi la iye yekha, chochokera m'thupi adzatuta chivundi; koma wakufesera kwa Mzimu, chochokera mu Mzimu adzatuta moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:2

Kotero kuti iye amene atsutsana nao ulamuliro, akaniza choikika ndi Mulungu; ndipo iwo akukaniza, adzadzitengera kulanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 16:24-25

Pomwepo Yesu anati kwa ophunzira ake, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikane yekha, natenge mtanda wake, nanditsate Ine.

Pakuti iye amene afuna kupulumutsa moyo wake adzautaya: koma iye amene ataya moyo wake chifukwa cha Ine, adzaupeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:12-13

Potero, okondedwa anga, monga momwe mumvera nthawi zonse, posati pokhapokha pokhala ine ndilipo, komatu makamaka tsopano pokhala ine palibe, gwirani ntchito yake ya chipulumutso chanu ndi mantha, ndi kunthunthumira;

pakuti wakuchita mwa inu kufuna ndi kuchita komwe, chifukwa cha kukoma mtima kwake, ndiye Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 11:25

nasankhula kuchitidwa zoipa pamodzi ndi anthu a Mulungu, kosati kukhala nazo zokondweretsa za zoipa nthawi;

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 30:21

ndipo makutu ako adzamva mau kumbuyo kwa iwe akuti, Njira ndi iyi, yendani inu m'menemo: potembenukira inu kulamanja, ndi potembenukira kulamanzere.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 1:7

Pakuti Mulungu sanatipatse mzimu wa mantha; komatu wa mphamvu ndi chikondi ndi chidziletso.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:16

Inu simunandisankhe Ine, koma Ine ndinakusankhani inu, ndipo ndinakuikani, kuti mukamuke inu ndi kubala chipatso, ndi kuti chipatso chanu chikhale; kuti chimene chilichonse mukapempha Atate m'dzina langa akakupatseni inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:26-27

Sinkhasinkha bwino mayendedwe a mapazi ako; njira zako zonse zikonzeke.

Usapatuke kudzanja lamanja kapena kulamanzere; suntha phazi lako kusiya zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 32:8

Ine ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo; ndidzakupangira ndi diso langa lakuyang'ana iwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 12:57

Ndipo inunso, pa nokha mulekeranji kuweruza kolungama?

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:17

Potero kwa iye amene adziwa kuchita bwino, ndipo sachita, kwa iye kuli tchimo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:11

Mwa Iye tinayesedwa akeake olandira cholowa, popeza tinakonzekeratu monga mwa chitsimikizo mtima cha Iye wakuchita zonse monga mwa uphungu wa chifuniro chake;

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 10:23

Inu Yehova, ndidziwa kuti njira ya munthu sili mwa iye mwini; sikuli kwa munthu woyenda kulongosola mapazi ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 3:15

umo anenamo, Lero ngati mudzamva mau ake, musaumitse mitima yanu, monga pa kupsetsa mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 12:36-37

Ndipo ndinena kwa inu, kuti mau onse opanda pake, amene anthu adzalankhula, adzawawerengera mlandu wake tsiku la kuweruza.

Pakuti udzayesedwa wolungama ndi mau ako, ndipo ndi mau ako omwe udzatsutsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 2:6-8

amene adzabwezera munthu aliyense kolingana ndi ntchito zake;

kwa iwo amene afunafuna ulemerero ndi ulemu ndi chisaonongeko, mwa kupirira pa ntchito zabwino, adzabwezera moyo wosatha;

koma kwa iwo andeu, ndi osamvera choonadi, koma amvera chosalungama, adzabwezera mkwiyo ndi kuzaza,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:29-31

chifukwa anada nzeru, sanafune kuopa Yehova;

kulandira mwambo wakusamalira machitidwe, chilungamo, chiweruzo ndi zolunjika;

anakana uphungu wanga, nanyoza kudzudzula kwanga konse;

momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao, nadzakhuta zolingalira zao.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 10:42

koma chisoweka chinthu chimodzi, pakuti Maria anasankha dera lokoma limene silidzachotsedwa kwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 5:29

Ha? Mwenzi akadakhala nao mtima wotere wakundiopa Ine, ndi kusunga malamulo anga masiku onse, kuti chiwakomere iwo ndi ana ao nthawi zonse!

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:26

Pakuti tikachimwa ife eni ake, titatha kulandira chidziwitso cha choonadi, siitsalanso nsembe ya kwa machimo,

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:22-24

kuti muvule, kunena za makhalidwe anu oyamba, munthu wakale, wovunda potsata zilakolako za chinyengo;

koma kuti mukonzeke, mukhale atsopano mu mzimu wa mtima wanu,

nimuvale munthu watsopano, amene analengedwa monga mwa Mulungu, m'chilungamo, ndi m'chiyero cha choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:12

Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka; koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Atate wabwino ndi wokhulupirika, ulemerero ndi ulemu zikhale kwa Inu! Ambuye, m'dzina la Yesu ndikubwera kwa Inu. Zikomo chifukwa munatilolenga ife m'chifaniziro chanu, ndi kutipatsa ufulu wosankha zabwino ndi zoyipa. Ambuye ndikupemphani kuti mulandire moyo wanga, mundipatse nzeru zosankha zoyenera zomene zingasinthe tsogolo langa, osati kudalira maganizo anga. "Pakuti pali njira yooneka yolungama kwa munthu, koma potsiriza pake ndiyo njira ya imfa." Ambuye, kudzera mwa Mzimu wanu Woyera nditha kuzindikira zomwe sizochokera kwa Inu, kuti ndisatsogoleredwe ndi thupi, koma ndiyende momvera ndi kukhala mogwirizana ndi mawu anu, chifukwa popanda Inu sindingathe kuchita chilichonse. Limbitsani mapazi anga ndi kunditsogolera m'njira zolungama. Nditetezani ku ziwembu ndi misampha ya mdani. M'dzina la Yesu. Ameni.