Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

NDIME ZA MULUNGU

Mulungu ndiye mlengi wako, mtetezi wako, wosamalira wako. Ndi wamphamvuzonse, wachifundo, wokhululuka, wabwino. Tingadziwe Mulungu kudzera m'mawu ake. Amakuikira mtima ndipo wakupangira dongosolo labwino pa moyo wako.

Amadziwa zonse zisanachitike. Ndi chikondi chosatha. Pakuti Ine Yehova ndine Mulungu wako, wakugwira dzanja lako lamanja, nanena ndi iwe, Usawopa; Ine ndikuthandiza. (Yesaya 41:13)

Choncho Mulungu nthawi zonse adzakhala nafe, timangofunika kumuyandikila. Iye ndiye mlengi ndi wosamalira zinthu zonse, amene anapulumutsa dziko kudzera mwa Mwana wake, Yesu Khristu.


Masalimo 50:14

“Koma perekani nsembe zanu zothokozera kwa Mulungu, ndipo muchite zimene mudalumbira kwa Wopambanazonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 100:1

Fuulani kwa Chauta ndi chimwemwe, inu maiko onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 47:7

Mulungu ndiye Mfumu ya dziko lonse lapansi. Imbani mwaluso nyimbo zotamanda.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 67:3

Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu, mitundu yonse ya anthu ikuyamikeni.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:1

Ndidzakuyamikani, Inu Mulungu wanga, mfumu yanga, ndidzalemekeza dzina lanu nthaŵi zonse mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 33:9

Mzinda umenewu udzamveketsa mbiri yanga yabwino, ndipo udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemu. Anthu a mitundu yonse pansi pano adzanditamanda ndi kundilemekeza pakumva za zabwino zonse zimene ndauchitira mzinda umenewu. Adzachita mantha ndi kunjenjemera, poona kuti mzindawo ndaupatsa madalitso ndi zokoma zosaŵerengeka.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:171

Pakamwa panga padzakutamandani, chifukwa mumandiphunzitsa malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:25

Chauta ngwamkulu, ngwoyenera kumtamanda kwambiri, ngwoyenera kumuwopa kupambana milungu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:3

Mulungu waika nyimbo yatsopano m'kamwa mwanga, nyimbo yake yotamanda Iye. Anthu ambiri adzaona zimenezi ndipo adzaopa, nadzakhulupirira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:1

Ndidzayamika Chauta nthaŵi zonse, pakamwa panga padzatamanda Iye kosalekeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 100:4

Loŵani pa zipata zake mukuthokoza, pitani m'mabwalo a Nyumba yake mukutamanda. Yamikani Chauta, lemekezani dzina lake!

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:15

Nchifukwa chake, kudzera mwa Yesu tiyeni tipereke kosalekeza mayamiko athu kwa Mulungu ngati nsembe. Ndiye kunena kuti tipereke ngati nsembe mau athu ovomereza dzina lake poyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:7

Imbirani Chauta mothokoza, imbirani Mulungu wathu nyimbo yokoma ndi pangwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 96:6

Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake. Mphamvu ndi kukongola zili m'Nyumba mwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 96:4

Chauta ngwamkulu, ngwoyenera kumtamanda kwambiri. Nwoyenera kumuwopa kupambana milungu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 75:9

Koma ine sindidzaleka kukondwera, ndidzaimba nyimbo zotamanda Mulungu wa Yakobe mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:6-7

Bwerani, timpembedze ndi kumlambira. Tiyeni tigwade pamaso pa Chauta Mlengi wathu.

Pakuti ndiye Mulungu wathu, ndipo ife ndife anthu a pa busa lake, ndife nkhosa zodyera m'manja mwake. Lero mukadamverako mau ake!

Mutu    |  Mabaibulo
Yona 2:9

Koma ine ndidzapereka nsembe kwa Inu ndi mau okuthokozani. Zimene ndidalonjeza ndidzazichita ndithu. Chipulumutso nchochokera kwa Inu Chauta.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:21

Pakamwa panga padzayamika Chauta, zamoyo zonse zitamande dzina lake loyera mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:27

Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi chimwemwe zili m'Nyumba mwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 148:2

Mtamandeni inu angelo ake onse, mtamandeni inu magulu a ankhondo ake onse!

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 4:24

Mulungu ndi mzimu, ndipo ompembedza Iye ayenera kumpembedza mwauzimu ndi moona.”

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 15:11

“Inu Chauta, kodi pali mulungu wina wofanafana nanu? Ndani amafanafana ndi Inu, amene muli aulemu chifukwa cha ungwiro wanu? Ndani amafanafana nanu, Inu amene muli oopsa chifukwa cha ntchito zanu zaulemu ndi zodabwitsa?

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 15:2

Chauta ndiye mphamvu zanga, ndiye amene ndimamuimbira, ndiye chipulumutso changa. Iye ndiye Mulungu wanga, ndipo ndidzamtamanda. Ndiye Mulungu wa atate anga, ndipo ndidzamuyamika kwakukulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 150:6

Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Chauta. Tamandani Chauta!

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 35:28

Tsono nanenso ndidzalalika za kulungama kwanu. Ndidzakutamandani masiku onse, Inu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:2

Tiyeni, tikafike pamaso pake, tikamthokoze, tiyeni tifuule kwa Iye ndi chimwemwe, timuimbire nyimbo zotamanda.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:1

Kondwerani mwa Chauta, inu anthu ake. Zoonadi ochita zolungama azitamanda.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 2:12

ponena mau akuti, “Ndidzasimbira abale anga za dzina lanu. Ndidzakutamandani pa msonkhano wa anthu anu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:3

Chauta ndi wamkulu ndi woyenera kumtamanda kwambiri, ndipo ukulu wake sitingathe kuumvetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 12:5

“Imbirani Chauta nyimbo zotamanda, pakuti wachita zazikulu. Zimenezi zidziŵike pa dziko lonse lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 29:2

Tamandani ulemerero wa dzina la Chauta. Mumpembedze mu ulemu wa ungwiro wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 78:4

Sitidzabisira ana ao, koma tidzafotokozera mbadwo wakutsogolo ntchito zotamandika za Chauta, tidzaŵasimbira mphamvu zake ndi zodabwitsa zimene wakhala akuchita.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 2:2

“Palibe woyera wina wofanafana ndi Chauta, palibe wina koma Iye yekha. Palibe thanthwe lina lotchinjiriza lofanafana ndi Mulungu wathu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 42:4

Mtima wanga umaŵawa ndikamakumbukira m'mene ndinkayendera ndi chinamtindi cha anthu, poŵatsogolera ku Nyumba ya Mulungu. Panali khwimbi la anthu ofuula mosangalala, akuimba nyimbo zothokoza ndipo akuchita chikondwerero.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 100:2

Tumikirani Chauta mosangalala. Bwerani pamaso pake mukuimba mokondwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 79:13

Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pa busa lanu, tidzakuthokozani mpaka muyaya, tidzakutamandani m'mibadwo yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 43:21

Amenewo ndi anthu amene ndidadzilengera, ndipo azindiimbira nyimbo zotamanda Ine.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 22:25

Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Zimene ndidalonjeza ndidzazichita pamaso pa onse okumverani.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 9:11

Imbani nyimbo zotamanda Chauta amene amakhala ku Ziyoni. Lalikani za ntchito zake kwa anthu a mitundu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:1

Tsono abale, popeza kuti Mulungu watichitira chifundo chachikulu chotere, ndikukupemphani kuti mupereke matupi anu omwe kuti akhale nsembe yamoyo, yopatulika, ndi yokondwetsa Mulungu. Imeneyi ikhale njira yanu yopembedzera Mulungu mwauzimu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:28-29

Popeza kuti talandira ufumu wosagwedezeka, tizithokoza Mulungu, ndipo pakutero timpembedze moyenera, mwaulemu ndi mwamantha.

Paja Mulungu wathu ndi moto wopsereza.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 19:5

Pambuyo pake ku mpando wachifumu uja kudachoka mau akuti, “Tamandani Mulungu wathu, inu nonse atumiki ake, inu nonse omuwopa, ang'onoang'ono ndi akuluakulu omwe.”

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 2:20

Pambuyo pake abusa aja adabwerera akuyamika ndi kutamanda Mulungu chifukwa cha zonse zimene anali atamva ndi kuziwona. Zonse zinali monga momwe mngelo uja adaaŵauzira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:17

Ndidzapereka kwa Inu nsembe yothokozera, ndidzapemphera potchula dzina la Inu, Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:16-17

Mau a Khristu akhazikike kwathunthu m'mitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana ndi nzeru zonse. Muziimbira Mulungu ndi chiyamiko m'mitima mwanu, pamene mukuimba masalimo, nyimbo zotamanda Mulungu ndi nyimbo zina zauzimu.

Chilichonse chimene mungachite, kaya nkulankhula, kaya nkugwira ntchito, muchichite m'dzina la Ambuye Yesu ndi kuthokoza Mulungu Atate kudzera mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 4:10

Apo Yesu adati, “Choka, Satana! Paja Malembo akuti, ‘Uzipembedza Ambuye, Mulungu wako, ndipo uziŵatumikira Iwo okha.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 86:9

Mitundu yonse ya anthu imene mwailenga idzabwera, idzakuŵeramirani, Inu Ambuye, ndipo idzalemekeza ukulu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:29

Tamandani ulemerero wa dzina la Chauta. Bwerani ndi zopereka, ndipo muloŵe m'mabwalo a Nyumba yake. Pembedzani Chauta waulemerero ndi woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 34:14

Musadzapembedze mulungu wina aliyense, chifukwa Chauta amene dzina lake ndi Kansanje, ndi Mulungu wansanjedi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:1

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga, moyo wanga wonse umuyamike potchula dzina lake loyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 22:3

Komabe Inu ndinu oyera, mumakhala pa mpando wanu waufumu, ndipo anthu anu Aisraele amakutamandani.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 4:11

“Inu Ambuye athu ndi Mulungu wathu, ndinu oyenera kulandira ulemerero, ulemu ndi mphamvu, pakuti ndinu mudalenga zinthu zonse. Mudafuna kuti zonsezo zikhalepo, ndipo zidalengedwa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 3:3

Paja ifeyo ndiye oumbala enieni, ife amene timapembedza Mulungu motsogoleredwa ndi Mzimu Woyera. Timanyadira Khristu Yesu, osadalira miyambo ya thupi chabe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:1-2

Bwerani, timuimbire Chauta. Tiyeni tifuule ndi chimwemwe kwa Iye, thanthwe lotipulumutsa.

Pa zaka makumi anai ndidaipidwa ndi mbadwo umenewo, choncho ndidati, “Ameneŵa ndi anthu osakhulupirika, sasamalako njira zanga.”

Choncho ndidakwiya nkulumbira kuti anthuwo sadzaloŵa ku malo anga ampumulo.

Tiyeni, tikafike pamaso pake, tikamthokoze, tiyeni tifuule kwa Iye ndi chimwemwe, timuimbire nyimbo zotamanda.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 29:11-12

Inu Ambuye, ndinu aakulu, amphamvu, aulemerero, opambana pa nkhondo ndiponso oposa pa ulemu, pakuti zonse zakumwamba ndi za pansi pano nzanu. Mfumu ndinu nokha, Inu Chauta, ndipo wolamulira zonse ndinu.

Chuma ndi ulemu zimachokera kwa Inu ndipo mumalamulira zonse, chifukwa muli ndi mphamvu zonse. Inu nokha mutha kukweza munthu ndi kumpatsa mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:7

Koma ine ndidzatha kuloŵa m'Nyumba mwanu chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu. Ndidzaŵeramitsa mutu pansi, kupembedza Inu m'Nyumba yanu yoyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 15:9

Amandipembedza inde, koma kupembedza kwaoko nkopanda phindu, chifukwa zimene amaphunzitsa ngati zophunzitsa zenizeni ndi malamulo a anthu chabe.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 29:13

Ambuye adati, “Anthu aŵa amati amapemphera kwa Ine, koma mau ao ndi opanda tanthauzo, ndipo mitima yao ili kutali ndi Ine. Chipembedzo chao ndi kungotsata chabe malamulo ongoŵaloŵeza pamtima, malamulo ochokera kwa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:4

Kondwa mwa Chauta, ndipo adzakupatsa zimene mtima wako ukukhumba.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:10-11

Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse, musalole kuti ndisiye kumvera malamulo anu.

Ndili ndi nzeru kupambana okalamba, pakuti ndimatsata malamulo anu.

Ndimaletsa miyendo yanga kuti isayende m'njira yoipa iliyonse, kuti choncho ndizisunga mau anu.

Sindisiyana nawo malangizo anu, pakuti Inu mudandiphunzitsa

mau anu ndi otsekemera kwambiri ndikaŵalaŵa. Amatsekemera kuposa uchi m'kamwa mwanga.

Ndimakhala ndi nzeru za kumvetsa chifukwa cha malamulo anu. Nchifukwa chake ndimadana ndi njira iliyonse yonyenga.

mau anu ndiye nyale ya mapazi anga, ndipo amaunikira njira yanga.

Ndalumbirira, ndipo ndatsimikiza kuti ndidzamvera malangizo anu olungama.

Ndazunzika koopsa, Chauta, patseni moyo, molingana ndi mau anu aja.

Chauta, landirani mapemphero anga oyamika, ndipo mundiphunzitse malangizo anu.

Moyo wanga uli m'zoopsa nthaŵi zonse, komabe sindiiŵala malamulo anu.

Ndasunga mau anu mumtima mwanga, kuti ndisakuchimwireni.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 138:1-2

Ndikukuthokozani Inu Chauta ndi mtima wanga wonse. Ndikuimba nyimbo zokutamandani pamaso pa milungu.

Ndikugwada moŵerama kumaso kwa Nyumba yanu yoyera. Ndikutamanda dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika, chifukwanso cha kukhulupirika kwanu. Mwakweza dzina lanu ndiponso malonjezo anu kupambana chinthu china chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:16

pakundipatula kuti ndikhale mtumiki wa Khristu Yesu kwa anthu a mitundu ina. Adandipatsa ntchito yolalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu ngati wansembe, kuti anthuwo akhale ngati nsembe yokomera Iye ndi yoperekedwa mwa Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 47:6-7

Imbani nyimbo zotamanda Mulungu, imbani nyimbo zotamanda. Imbani nyimbo zotamanda mfumu yathu, imbani nyimbo zotamanda.

Mulungu ndiye Mfumu ya dziko lonse lapansi. Imbani mwaluso nyimbo zotamanda.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 6:13

Muziwopa Chauta, Mulungu wanu. Muzipembedza Iye yekha, ndipo mukamalumbira, muzitchula dzina lake lokha.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 7:11-12

Angelo onse adaimirira kuzungulira mpando wachifumu uja, kuzunguliranso Akuluakulu aja ndi Zamoyo zinai zija. Angelowo adadzigwetsa chafufumimba patsogolo pa mpando wachifumuwo, napembedza Mulungu.

Adati, “Amen! Mulungu wathu alandire matamando, ulemerero, nzeru, chiyamiko, ulemu, mphamvu ndi nyonga mpaka muyaya. Amen.”

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 10:31

Tsono, kaya mulikudya, kaya mulikumwa, kaya mukuchita chilichonse, muzichita zonse kuti mulemekeze Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 6:3

Aserafiwo ankafuulirana kuti, “Ngwoyera, ngwoyera, ngwoyera Chauta Wamphamvuzonse, ulemerero wake wadzaza dziko lonse lapansi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 63:1-3

Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, ndimakufunafunani. Mtima wanga ukumva ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka Inu ngati dziko louma, loguga ndi lopanda madzi.

Iwo adzaperekedwa kuti akaphedwe ku nkhondo, motero adzasanduka chakudya cha nkhandwe.

Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu. Onse olumbirira Iye, adzamtamanda, koma pakamwa pa anthu abodza padzatsekedwa.

Ndikukhumbira kukuwonani m'malo anu oyera ndi kuwona mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.

Ndidzakutamandani chifukwa chikondi chanu nchabwino kupambana moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:30

Tsono ataimba nyimbo yotamanda Mulungu, onse adatuluka nkumapita ku Phiri la Olivi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 69:30-31

Ndidzatamanda dzina la Mulungu pomuimbira nyimbo, ndidzalalika ukulu wake pomuthokoza.

Zimenezi zidzakondwetsa Chauta kupambana nsembe, ngakhale nsembe ya ng'ombe yamphongo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:3

Pakuti Chauta ndiye Mulungu wamkulu, ndiye Mfumu yaikulu yopambana milungu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 4:8

Apo Yesu adati, “Malembo akuti, ‘Uzipembedza Ambuye Mulungu wako, ndipo uziŵatumikira Iwo okha.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:25

Adasiya zoona za Mulungu namatsata zabodza. Adayamba kupembedza ndi kutumikira zolengedwa m'malo mwa kupembedza ndi kutumikira Mlengi mwini, amene ali woyenera kumlemekeza mpaka muyaya. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 15:4

Ambuye, ndani angapande kukuwopani ndi kutamanda dzina lanu? Paja ndinu nokha oyera. Anthu a mitundu yonse adzabwera nkudzakupembedzani, popeza kuti ntchito zanu zolungama zaonekera poyera.”

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Zikomo Ambuye, inu ndinu wochiritsa wanga, wopereka wanga, ndi mlonda wanga. Inu ndinu amene mumalowerera nkhondo zanga, ndi kunditsogolera kuchoka pa ulemerero kupita pa ulemerero. M'dzina lamphamvu la Yesu, ndimabwera kwa inu kukulambirani ndi kukudalitsani chifukwa cha chikondi chanu chachikulu ndi chifundo chanu chosatha. Mfumu yanga, ndikudalitsani ndi kukukwezani chifukwa mwandikhululukira, mwandipulumutsa, mwandiyang'ana ndi chisomo Mulungu. Inu mumachita zizindikiro kumwamba ndi pano padziko lapansi, munatsegula nyanja pakati. Aa wodalitsidwa, Woyera wa Israeli! Aa Mulungu wodalitsidwa pakati pa mitundu yonse, iwo akukutamandani ndi kudalitsa dzina lanu, lomwe lili pamwamba pa dzina lililonse ndi kulengeza kuti ndinu Mfumu yayikulu. Mulungu ndikupemphani kuti nthawi zonse chiyamiko chanu chikhale mkamwa mwanga nthawi zonse. Mawu anu amati: "Wodalitsika Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene anatidalitsa ndi madalitso onse auzimu m'malo akumwamba mwa Khristu." Zikomo chifukwa chifundo chanu ndi cha mibadwo ndi mibadwo, inu ndinu Mulungu wanga, Mfumu yanga ndipo palibe chabwino kunja kwa inu. Inu ndinu mlengi wa kumwamba ndi dziko lapansi, dzina lanu lokha ndilo lokwezeka, onse oyera mtima anu atamande ndi kuimba ndi chimwemwe chifukwa ntchito zanu ndi zodabwitsa ndi zosawerengeka monga mchenga wa m'nyanja. M'dzina la Yesu. Ameni!