Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

150 Maupangiri a Mulungu Ochokera m'Baibulo


Miyambo 2:6

Paja Chauta ndiye amapatsa nzeru, Iye ndiye kasupe wa kudziŵa zinthu ndi wa kumvetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:5

Wina mwa inu akasoŵa nzeru, apemphe kwa Mulungu, ndipo adzalandira, pakuti Mulungu amapereka kwa onse mwaufulu ndi mosatonzera.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 9:10

Kulemekeza Chauta ndiye chiyambi cha nzeru, kudziŵa Woyera uja nkukhala womvetsa bwino zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:13-14

Ngwodala munthu amene wapeza nzeru, amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,

pakuti phindu la nzeru nloposa phindu la siliva, nloposanso ndi phindu la golide lomwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:7

Kuwopa Chauta ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru ndiye zimanyoza nzeru ndi malangizo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 111:10

Kuwopa Chauta ndiye chiyambi cha nzeru. Wotsata malamulo ake amakhala ndi nzeru zenizeni. Chauta ndi wotamandika mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:7

Chachikulu pa nzeru ndi ichi: Kaya nchiyani chimene ungapate, peza nzeruyo, usalephere kupata khalidwe la kumvetsa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 12:13

“Koma Mulungu ali ndi nzeru ndi mphamvu zopambana. Ali ndi uphungu wabwino, ndi kumvetsa zinthu zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:20

Uzimvera malangizo ndi kuvomera mwambo, kuti ukhale ndi nzeru m'tsogolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:17

ndipo ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate aulemerero, akuninkheni Mzimu Woyera, amene adzakupatsani nzeru, nadzaulula Mulungu kwa inu, kuti mumdziŵe kwenikweni.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:11

Nzerutu ndi yabwino kuposa miyala yamtengowapatali. Zonse zimene ungazilakelake sizingafanefane ndi nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:17

Koma nzeru zochokera Kumwamba, poyamba nzangwiro, kuwonjeza apo nzamtendere, zofatsa ndi zomvera bwino. Ndi za chifundo chambiri, ndipo zipatso zake zabwino nzochuluka. Nzeruzo sizikondera kapena kuchita chiphamaso.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:10-11

Landirani malangizo anga m'malo mwa siliva, funitsitsani kudziŵa zinthu, osati kuthamangira golide wabwino kwambiri.

Nzerutu ndi yabwino kuposa miyala yamtengowapatali. Zonse zimene ungazilakelake sizingafanefane ndi nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:16

Kupata nzeru kumapambana kupata golide. Kumvetsa zinthu nkwabwino, kumapambana kukhala ndi siliva.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 2:2-3

Ndikufuna kuti zimenezi ziŵalimbitse mtima, ndipo azilunzana pamodzi m'chikondi, azikhala odzaza ndi nzeru zomvetsa zinthu. Motero adzatha kudziŵa mozama chinsinsi cha Mulungu chonena za Khristu.

Mudafa pamodzi ndi Khristu, ndiye kuti simulamulidwanso ndi miyambo ya dziko lapansi. Tsono bwanji mukuchita ngati kuti moyo wanu ukudalirabe zapansipano? Bwanji mukuŵamvera malamulo onga aŵa akuti,

“Usagwire chakuti”, “Usakhudze chakuti”?

Malamulo ameneŵa ndi zophunzitsa zimenezi ndi za anthu chabe, ndipo zimangokhudza zinthu zimene zimatha, anthu akamazigwiritsa ntchito.

Kwinaku mauwo amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamula anthu zambiri pa za kupembedza, za kudzichepetsa ndi za kuzunza thupi lao. Komabe malamulowo alibe phindu, ndipo sathandiza konse kugonjetsa khalidwe longosangalatsa thupi.

Mwa Iyeyu mudzapeza chuma chonse chobisika, ndiye kuti nzeru ndi luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 1:25

Pajatu chimene chimaoneka ngati kupusa kwa Mulungu, nchanzeru kupambana nzeru za anthu. Ndipo chimene chimaoneka ngati kufooka kwa Mulungu, nchamphamvu kupambana mphamvu za anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:15

Munthu wochenjera amafuna kuphunzirabe zambiri, amafunitsitsa kudziŵa bwino zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:23

Kwa chitsiru kulakwa kumakhala ngati maseŵera, koma kwa munthu womvetsa zinthu kuchita zanzeru ndiye kumapatsa chimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 28:28

Choncho adauza munthu kuti, ‘Kuwopa Ambuye ndiye nzeru zimenezo, kuthaŵa zoipa ndiye luntha limenelo.’ ” Yobe

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 7:12

Chitetezo cha nzeru chili ngati chitetezo cha ndalama. Koma kudziŵa zinthu kukuposerapo, chifukwa nzeru zimasunga moyo wa amene ali nazo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:10

Chipongwe cha osasamala za anzao chimadzetsa mkangano, koma omvera malangizo a anzao ndiwo ali ndi nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:8

Nzeru za munthu wochenjera zagona pa kuzindikira bwino njira zake, koma zitsiru zimanyengedwa nkupusa kwao komwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:2

Kunyada kukaloŵa, pamafikanso manyazi, koma pali kudzichepetsa, palinso nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 2:6-7

Komabe pakati pa anthu okhwima m'chikhulupiriro, timalankhula zanzeru. Koma nzeruzo si za masiku anozi, kapena za akulu olamulira dziko lino lapansi, amene mphamvu zao nzodzatha.

Nzeru zimene timalankhula, ndi nzeru za Mulungu, zachinsinsi, zobisika kwa anthu. Mulungu asanalenge dziko lapansi, adaakonzeratu zimenezi kuti atipatse ulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:5-6

Usaiŵale mau a pakamwa pangaŵa, usatayane nawo, Ukhale ndi nzeru, ndiponso khalidwe la kumvetsa zinthu.

Usaisiye nzeru, ndipo idzakusunga. Uziikonda, ndipo idzakuteteza.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:2

Uzitchera khutu ku nzeru, uziikapo mtima pa kumvetsa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:11

Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera pa njira za moyo wolungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 33:6

Adzakupatsani mtendere wokhazikika pa nthaŵi yanu. Adzakuninkhaninso chipulumutso chachikulu, luntha lambiri ndi nzerunso zambiri. Kuwopa Chauta ndiko kumapezetsa chuma chimenechi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:1-2

Kodi suja nzeru imaitana? Suja nzeru zomvetsera zinthu zimakweza mau ake?

Landirani malangizo anga m'malo mwa siliva, funitsitsani kudziŵa zinthu, osati kuthamangira golide wabwino kwambiri.

Nzerutu ndi yabwino kuposa miyala yamtengowapatali. Zonse zimene ungazilakelake sizingafanefane ndi nzeru.

Ine nzeru ndimakhalira limodzi ndi kuchenjera. Ndimadziŵa zinthu ndipo ndimaganiza moyenera.

Kuwopa Chauta nkudana ndi zoipa. Kunyada, kudzitama, kuchita zoipa ndi kulankhula zonyenga, zonsezo ndimadana nazo.

Ndili ndi uphungu ndi maganizo abwino. Ndimamvetsa bwino zinthu, ndilinso ndi mphamvu.

Ndimathandiza mafumu polamulira ndine, olamulira ndimaŵathandiza ndine kulamula zolungama.

Ndine ndimathandiza akalonga polamula, ndine ndimathandiza akuluakulu poweruza m'dziko.

Anthu ondikonda, ine nzeru ndimaŵakonda, anthu ondifunafuna mosamala, amandipeza.

Ndili nacho chuma, ndili nawo ulemu, chuma chosatha ndiponso kukhuphuka konkirankira.

Zimene mumalandira kwa ine nzokoma kuposa golide, ngakhale golide wosalala. Phindu lochokera mwa ine nloposa siliva wabwino zedi.

Nzeru imakhala pa zitunda m'mbali mwa njira, imakaima pa mphambano za miseu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:13

Uŵasamale zedi, pakuti moyo wako wagona pamenepo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 23:12

Mtima wako ukhale pa malangizo, ndipo makutu ako azimvetsera mau anzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:5

Ndi oti wanzeru akaŵamva, aonjezere kuphunzira kwake, ndipo munthu womvetsa zinthu apate luso,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:66

Patseni luntha ndi nzeru, chifukwa ndimakhulupirira malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:35-36

Paja wondipeza ine, wapeza moyo, ndipo amapeza kuyanja pamaso pa Chauta.

Koma wosandipeza ine, akudzipweteka ameneyo. Onse odana ndi ine, ngokonda imfa amenewo.”

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 3:15

Ukudziŵanso kuti kuyambira ukali mwana waŵazoloŵera Malembo Oyera, amene angathe kukupatsa nzeru zopulumukira pakukhulupirira Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 9:9

Wanzeru ukamlangiza, adzakhala wanzeru koposa. Munthu wochita chilungamo ukamuphunzitsa, adzadziŵa zambiri koposa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:7

Mau a Chauta ngangwiro, amapatsa munthu moyo watsopano. Umboni wa Chauta ndi wokhulupirika, umaŵapatsa nzeru amene alibe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:7

Usamadziwona ngati wanzeru. Uziwopa Chauta, ndipo uleke zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:20-21

Mwana wanga, mvetsetsa mau anga. Tchera khutu ku zimene ndikunena.

Zisachoke m'mutu mwakomu, uzisunge bwino mumtima mwako.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 22:17

Utchere khutu lako, umve mau a anthu anzeru, uike mtima wako pa zophunzitsa zanga, kuti uzidziŵe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:97-98

Ndimakonda malamulo anu kwambiri, ndimasinkhasinkha za malamulowo tsiku lonse.

Malamulo anu amandisandutsa wanzeru kuposa adani anga, popeza kuti malamulowo ndili nawo nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:21

Mwana wanga, usunge nzeru yeniyeni usunge mkhalidwe wa kulingalira bwino, ziŵiri zimenezi zisakuthaŵe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:14

Mtima wa munthu womvetsa zinthu umafunitsitsa ndithu kudziŵa zambiri, koma m'kamwa mwa anthu opusa zauchitsiru zili pha!

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 28:12-13

“Koma nzeru zingapezeke kuti? Luntha lingapezeke kuti?

Anthu sadziŵa kufunika kwake kwa nzeruzo, ndipo sizipezeka pa dziko lino lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:3-4

Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu a mtima wodziŵa zinthu.

Ndinkayenda m'mbali mwa munda wa munthu waulesi, m'mbali mwa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.

M'minda monsemo munali mutamera minga yokhayokha, m'nthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utagwa.

Tsono nditaona, ndidayamba kuganizirapo pa zimenezo, nditayang'ana, ndidatolapo phunziro ili:

Ukati, “Taimani ndigoneko pang'ono,” kapena “Ndiwodzereko chabe,” kapena “Ndingopumulako pang'ono,”

umphaŵi udzakufikira monga mbala, kusauka kudzakupeza ngati mbala yachifwamba.

Wodziŵa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chokondweretsa ndi cha mtengo wapatali.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:13-14

Ndani adalamulirapo maganizo a Chauta? Ndani adamphunzitsapo kanthu ngati mlangizi wake?

Kodi Chauta adapemphapo nzeru kwa yani, kuti adziŵe zinthu? Ndani adamuphunzitsa kuweruza molungama? Ndani adamphunzitsa kudziŵa zinthu? Ndani adamlangiza njira ya kumvetsa zinthu?

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:10-11

Nzeru zidzaloŵa mumtima mwako, kudziŵa zinthu kudzakusangalatsa.

Kuganiziratu zam'tsogolo kudzakusunga, kumvetsa zinthu kudzakuteteza.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 4:5

Mayendedwe anu pakati pa anthu akunja azikhala anzeru, ndipo muzichita changu, osataya nthaŵi pachabe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 1:1-2

Ngwodala munthu wosatsata uphungu wa anthu oipa, wosatsanzira mayendedwe a anthu ochimwa, wosakhala nawo m'gulu la anthu onyoza Mulungu,

koma wokondwerera kumvera malamulo a Chauta, nkumasinkhasinkha za malamulowo usana ndi usiku.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 90:12

Tsono tiphunzitseni kuŵerenga masiku athu, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:33

Muzimva malangizo, kuti muzikhala anzeru, musamanyozere mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:27

Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziŵa zinthu, munthu wodekha mtima ndiye womvetsa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:8

Amene amakonda nzeru amadzichitira zabwino mwiniwakeyo. Amene ali womvetsa, zinthu zidzamuyendera bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 3:19

Zoonadi nzeru za anthu odalira zapansipano, nzopusa pamaso pa Mulungu. Pajatu Malembo akuti, “Mulungu amakola anthu anzeru m'kuchenjera kwao.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 28:5

Anthu oipa samvetsa kuti chilungamo nchiyani, koma amene amatsata kufuna kwa Chauta amachimvetsa kwathunthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 32:8

Chauta akuti, “Ndidzakudziŵitsa ndi kukuphunzitsa njira imene uyenera kuyendamo. Ndidzakulangiza ndi kukuyang'anira.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:6

Wonyoza anzake amafunafuna nzeru osaipeza, koma munthu womvetsa amadziŵa bwino zinthu msanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:33

Kuwopa Chauta kumaphunzitsa nzeru, ndipo ndi kudzichepetsa ndi ulemu, chili patsogolo nkudzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:15-17

Samalirani bwino mayendedwe anu. Musayende monga anthu opanda nzeru, koma monga anthu anzeru.

Mukhale achangu, osataya nthaŵi yanu pachabe, pakuti masiku ano ngoipa.

Nchifukwa chake musakhale opusa, koma dziŵani zimene Ambuye afuna kuti muchite.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:14

Ndili ndi uphungu ndi maganizo abwino. Ndimamvetsa bwino zinthu, ndilinso ndi mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 6:6-8

Pita kwa nyerere, mlesi iwe. Kapenyetsetse makhalidwe ake, ukaphunzireko nzeru.

Ilibe ndi mfumu yomwe, ilibe kapitao kapena wolamulira.

Komabe imakonzeratu chakudya chake m'malimwe, ndipo imatuta chakudyacho m'masika.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:2

Chitsiru sichisamalako za kumvetsa zinthu. Koma chimangolankhula za maganizo ake okha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:4-5

Mundidziŵitse njira zanu, Inu Chauta, mundiphunzitse kuchita kufuna kwanu.

Munditsogolere m'choona chanu ndi kundilangiza, pakuti Inu ndinu Mulungu Mpulumutsi wanga, ndimadalira Inu masiku onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 55:8-9

Chauta akunena kuti, “Maganizo anga ndi maganizo anu si amodzimodzi, ndipo zochita zanga ndi zochita zanu si zimodzimodzi.

Monga momwe mlengalenga uliri kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:8

Munthu wa mtima wanzeru adzasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 4:29

Mulungu adapatsa Solomoni nzeru ndi luntha losaneneka, nzeru zake zinali zopanda malire.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:1

Munthu wokonda mwambo amakonda kudziŵa zinthu, koma wodana ndi chidzudzulo ngwopusa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:144

Malamulo anu ndi olungama mpaka muyaya, patseni nzeru zomvetsa kuti ndizikhala ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 5:12-13

Amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chao sichiphula kanthu.

Amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwao, amathetsa msanga zimene akapsala adakonza kuti achite.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:21

Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amatsata zolungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 10:12

Mau a pakamwa pa munthu wanzeru amakondweretsa, koma pakamwa pa chitsiru mpoononga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:1

Mwana wanga, uvomere mau anga, ndi kusunga bwino malamulo anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:20-21

Nzeru ikufuula mu mseu, ikulankhula mokweza mau m'misika.

Ikufuula pa mphambano za miseu, ikulankhula pa zipata za mzinda, kuti,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:33-34

Muzimva malangizo, kuti muzikhala anzeru, musamanyozere mau anga.

Ngwodala munthu amene amatchera khutu kwa ine, amene amakhala pakhomo panga tsiku ndi tsiku, amene amadikira pa chitseko changa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 2:26

Pajatu munthu wokondweretsa Mulungu, Mulunguyo amamsandutsa waluntha, wanzeru ndi wosangalala. Koma wochimwa amampatsa ntchito yokunkha ndi younjika zinthu, kenaka zonsezo nkuzipatsa munthu wokondwetsa Mulungu. Zimenezinso nzopanda phindu, ndipo kuyesa kuzimvetsa nkungodzivuta chabe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:1-2

Ana inu, mverani malangizo a atate anu, tcherani khutu, kuti mupate nzeru zodziŵira zinthu.

Mwana wanga, umvere ndi kuvomera zimene ndikunena. Ukatero, zaka za moyo wako zidzachuluka.

Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera pa njira za moyo wolungama.

Ukamayenda, mapazi ako sazidzaombana. Ukamathamanga, sudzakhumudwa ai.

Uŵasamale zedi, pakuti moyo wako wagona pamenepo.

Usayende m'njira za anthu oipa, usatsate m'mapazi mwa anthu ochimwa.

Njira zao uzipewe, usapitemo konse. Uzilambalale, ndi kungozipitirira.

Iwo ajatu sangagone, mpaka atachita ndithu choipa. Tulo sangatiwone, mpaka atakhumudwitsapo munthu.

Paja kuchita zoipa ndiye chakudya chao, kuchita ndeu ndiye chakumwa chao.

Koma njira ya anthu okondweretsa Mulungu, ili ngati kuŵala kwa mbandakucha, kumene kumanka kukukulirakulira mpaka dzuŵa litafika pamutu.

Njira ya anthu oipa ili ngati mdima wandiweyani. Satha kuzindikira kuti aphunthwa pa chiyani.

Ine ndikukupatsani malamulo abwino, musasiye zimene ndikukuphunzitsani.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 73:24

Mumandiwongolera ndi malangizo anu, pambuyo pake mudzandilandira ku ulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:15

Pali golide ndi miyala yambirimbiri yamtengowapatali, koma mau olankhula zanzeru ali ndi mtengo woposa zonsezo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:130

Kufotokozera mau anu kumakhala ngati kuŵala, kumapatsa nzeru za kumvetsa kwa anthu opanda nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 5:21

Tsoka kwa amene amadziwona ngati anzeru ndipo amadziyesa ochenjera!

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:14

Udziŵe kuti nzeru ndi yoteronso mumtima mwako. Ukaipeza, zinthu zidzakuyendera bwino m'tsogolo, ndipo chikhulupiriro chako sichidzakhala chachabe.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 3:9

Nchifukwa chake mundipatse mtumiki wanune nzeru zolamulira anthu anu, kuti ndizidziŵa kusiyanitsa zabwino ndi zoipa. Nanga popanda nzeruzo ndani angathe kulamulira mtundu waukulu chotere wa anthu anu?”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:10

Landirani malangizo anga m'malo mwa siliva, funitsitsani kudziŵa zinthu, osati kuthamangira golide wabwino kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:14

Anzeru amakundika nzeru, koma kubwebwetuka kwa chitsiru kumadzetsa chiwonongeko.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:1

Mwana wanzeru amamvera malangizo a atate ake, koma wonyoza samvetsera akamamdzudzula.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 1:5-6

Tsono muyesetse kuchita khama kuwonjezera makhalidwe abwino pa chikhulupiriro chanu, ndi nzeru zoona pa makhalidwe anu abwinowo.

Muwonjezerepo kudziletsa pa nzeru zoonazo, kulimbika pa kudziletsa kwanu, ndiponso kupembedza Mulungu pa kulimbika kwanuko.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:99

Ndili ndi nzeru za kumvetsa kupambana aphunzitsi anga onse, pakuti ndimasinkhasinkha za malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:3-4

Khalidwe la kudzipereka ndi kukhulupirika zisakuthaŵe, makhalidwe ameneŵa uziyenda nawo ngati mkanda wam'khosi, uŵalembe mumtima mwako.

Usamakangane ndi munthu popanda chifukwa pamene iyeyo sadakuchite choipa chilichonse.

Usachite naye nsanje munthu wachiwawa, usatsanzireko khalidwe lake lililonse.

Paja Chauta amanyansidwa ndi munthu woipa, koma olungama okha amayanjana nawo.

Chauta amatemberera nyumba ya anthu oipa, koma malo okhalamo anthu abwino amaŵadalitsa.

Anthu onyoza, Iye amaŵanyoza, koma odzichepetsa Iye amaŵakomera mtima.

Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

Choncho udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi pa anthunso.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:23

Mtima wa munthu wanzeru umamlankhulitsa mau ochenjera, nzeruzo zimakulitsa mphamvu ya mau ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:30

Munthu wabwino amalankhula zanzeru, pakamwa pake pamatuluka zachilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 5:1-2

Mwana wanga, umvetsere bwino zanzeru ndikukuuzazi, utchere khutu kwa ine womvetsa bwino zinthu,

Mwinanso alendo adzadyerera chuma chako, phindu la ntchito zako lidzagwa m'manja mwa munthu wachilendo.

Ndipo potsiriza pa moyo wako udzalira chokuwa, thupi lako lonse litatheratu.

Pamenepo iwe udzangoti, “Kalanga ine, ndinkadana nkusunga mwambo, mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!

Sindidamvere mau a aphunzitsi anga, sindidatchere khutu kwa alangizi anga.

Pang'onong'ono, bwenzi nditaonongekeratu pakati pa mpingo wonse utasonkhana.”

Iwe, uzimwera m'chitsime chakochako, ndiye kuti khala wokhulupirika kwa mkazi wako.

Kodi ana ako azingoti mbwee ponseponse ngati madzi ongoyenda m'miseu?

Anawo akhale a iwe wekha, osatinso uŵagaŵane ndi alendo.

Uzikhutira ndi mkazi wako, uzikondwa ndi mkazi wa unyamata wako.

Iye uja ngwokongola ngati mbaŵala, ndi wa maonekedwe osiririka ngati mbalale. Uzikhutitsidwa ndi maŵere ake nthaŵi zonse, uzikokeka ndi chikondi chake pa moyo wako wonse.

kuti uziganiza mochenjera, ndipo pakamwa pako pazilankhula zanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:19-20

Pamene adakhazikitsa dziko lapansi, Chauta adaonetsa nzeru. Pamene adakhazikitsa zakumwamba, adaonetsa nzeru za kumvetsa bwino.

Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka, ndipo udzakhala ndi moyo wabwino kwambiri.

Pamene adatumphutsa madzi kuchoka kunsi kwa dziko, ndipo mitambo idagwetsa mvula, adaonetsa nzeru zodziŵa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:12

Nzeruyo idzakupulumutsa ku mayendedwe oipa, idzakuteteza kwa amtherakuŵiri,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:7

Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru, koma mitima ya zitsiru siitero.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:13-14

Mwana wanga, uzidya uchi poti ndi wabwino, madzi a m'chisa cha njuchi ndi ozuna ukaŵalaŵa.

Udziŵe kuti nzeru ndi yoteronso mumtima mwako. Ukaipeza, zinthu zidzakuyendera bwino m'tsogolo, ndipo chikhulupiriro chako sichidzakhala chachabe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:20

Munthu wovomera malangizo, zinthu zidzamuyendera bwino, ndi wodala amene amadalira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:8

Munthu amamuyamika malinga ndi nzeru zake, koma munthu wa mtima wokhota amanyozeka.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 32:8

Koma mzimu wa Mphambe ndiwo umaloŵa mwa anthu ndi kuŵapatsa nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:2-4

Ngothandiza kuti anthu adziŵe nzeru ndi mwambo, kuti amvetse mau a matanthauzo ozama,

Nzeru ikufuula mu mseu, ikulankhula mokweza mau m'misika.

Ikufuula pa mphambano za miseu, ikulankhula pa zipata za mzinda, kuti,

“Kodi anthu osachangamukanu, mudzakondwerabe kupusaku mpaka liti? Kodi anthu onyodola, adzakhalabe akunyodola mpaka liti? Nanga opusa adzakana kuphunzira zanzeru mpaka liti?

Musamale kudzudzula kwangaku, ine ndikuuzani maganizo anga, ndi kukudziŵitsani mau anga.

Paja ine ndidaakuitanani, inu nkukana kumvera, ndidaati ndikuthandizeni, koma popanda wosamalako.

Uphungu wanga simudaulabadire, kudzudzula kwanga simudakusamale.

Ndiye inenso ndidzakusekani, mukadzagwa m'mavuto, ndidzakunyodolani, mukadzazunguzika ndi mantha,

pamene mantha adzakukunthani ngati namondwe, pamene tsoka lidzakufikirani ngati kamvulumvulu, pamene mavuto ndi masautso adzakugwerani.

Tsono mudzandiitana, koma ine sindidzaitaŵa, mudzandifunafuna mwakhama, koma simudzandipeza.

Popeza kuti mudadana ndi nzeru, ndipo simudasankhe kuwopa Chauta,

kuti alandire mwambo wochita zinthu mwanzeru, akhale angwiro, achilungamo ndi osakondera.

popeza kuti simudasamale malangizo anga, ndipo mudanyoza kudzudzula kwanga konse,

basitu tsono mudzadya zipatso zoyenera ntchito zanuzo, mudzakhuta zoipa zimene munkafuna kuŵachita ena.

Anthu opusa amaphedwa chifukwa cha kusokera kwao. Zitsiru zimadziwononga zokha nkudzitama kwao.

Koma amene amamvera ine adzakhala pabwino, adzakhala mosatekeseka, osaopa choipa chilichonse”.

Ngophunzitsa anthu wamba nzeru za kuchenjera, ndi achinyamata kudziŵa zinthu ndi kulingalira bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 23:15-16

Mwana wanga, mtima wako ukakhala wanzeru, nanenso mtima wanga udzasangalala.

Mtima wanga udzakondwa ndikadzakumva ukulankhula zolungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 49:3

Zosinkhasinkha za mtima wanga zidzakhala zakuya, ndipo ndidzalankhula zanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 1:30

Mulungu ndiye adakulunzanitsani ndi Khristu Yesu, ndipo adamsandutsa kuti akhale nzeru yathu. Chifukwa cha Yesu, timapezeka olungama pamaso pa Mulungu. Ndi Yesuyo amene amatisandutsa anthu akeake a Mulungu, ndiye amatipulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:13

Pakamwa pa munthu womvetsa zinthu pamatuluka zanzeru, koma pamsana pa munthu wopanda nzeru sipachoka tsatsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:30

Kukhala moyo wangwiro kumapezetsa moyo, koma kusatsata malamulo kumaononga moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:2

Si bwino kuti munthu akhale wosadziŵa zinthu, ndipo munthu woyenda mofulumira dziŵi amasokera.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:20

Woyenda ndi anthu anzeru nayenso amakhala ndi nzeru, koma woyenda ndi zitsiru adzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:11

Nzeru zimapatsa munthu mtima wosakwiya msanga, ulemerero wake wagona pa kusalabadako za chipongwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:3

Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu a mtima wodziŵa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:19

Mau akachuluka, zolakwa sizisoŵa, koma amene amasunga pakamwa ndi wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:24

Mayendedwe a munthu amaŵalamula ndi Chauta: Tsono munthu angadziŵe bwanji njira yake?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:8

Malangizo a Chauta ndi olungama, amasangalatsa mtima. Malamulo a Chauta ndi olungama, amapatsa mtima womvetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:32

Munthu wosapsa mtima msanga amapambana wankhondo, amene amadzigwira mtima amapambana msilikali wogonjetsa mzinda.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:25

Ukamenya munthu wonyoza anzake, adzachenjererapo. Ukadzudzula munthu womvetsa bwino zinthu, adzapindulapo nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 49:15

Koma Mulungu adzaombola moyo wanga ku ulamuliro wa manda, sindidzaopa, pakuti Iye adzandilandira.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:10

Munthu wanzeru amamva kamodzi, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 28:26

Samvazaanzake nchitsiru, koma wotsata nzeru za ena adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:3

Kupusa kwake kwa munthu kukamgwetsa m'chiwonongeko, mtima wake umadzakwiyira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 8:1

Ndani angafanefane ndi munthu wanzeru? Ndani angadziŵe kutanthauza zinthu? Munthu nzeru zake zimampatsa chimwemwe, ndipo ukali umachoka pankhope pake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:125

Ndine mtumiki wanu, mundipatse nzeru zomvetsa, kuti ndizidziŵa malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:3-4

Ndikutitu upemphe mtima wozindikira zinthu, ndi kupemba kuti ukhale womvetsa zinthu.

Uziifunafuna nzeruyo ngati siliva, ndi kumaiwunguza ngati chuma chobisika.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:18

Uzimlanga mwana wako chikhulupiriro chikadalipo, ukapanda kutero, wamuwononga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:27

Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mau opatsa nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:18

Ukakonzekera kuchita zinthu, uziyamba wafunsa. Usanamenye nkhondo, uyambe wapempha malangizo oyenera.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 2:10-12

Ifeyo Mulungu adatiwululira zimenezi mwa Mzimu Woyera. Pajatu Mzimuyo amadziŵa zinthu zonse kotheratu, ngakhalenso maganizo ozama a Mulungu.

Kodi za munthu angazidziŵe ndani, osakhala mzimu wa mwiniwake yemweyo umene uli mwa iyeyo? Momwemonso palibe munthu amene angadziŵe za Mulungu, koma Mzimu wa Mulungu Mwini.

Ife sitidalandire mzimu wa dziko lino lapansi, koma tidalandira Mzimu Woyera wochokera kwa Mulungu, kuti adzatithandize kumvetsa zimene Mulunguyo adatipatsa mwaulere.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:5

Udzipereke m'manja mwa Chauta, umukhulupirire ndipo Iye adzakusamalira.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:5

Inu osadziŵa kanthunu, phunzirani nzeru, inu opusanu, khalani tcheru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 25:12

Kwa munthu womvetsera bwino, kudzudzula kuli ngati mphete yagolide, kapena chokongoletsera china chagolide.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:25-27

Maso ako aziyang'ana kutsogolo molunjika, uzipenya kutsogolo osacheukacheuka.

Uzisamala m'mene mukupita mapazi ako, ndipo njira zako zonse zidzakhala zosapeneketsa.

Usapatukire kumanja kapena kumanzere, usayende pamene pali choipa chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:31

Pakamwa pa wochita chilungamo pamatuluka zanzeru, koma lilime lokhota adzalidula.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 90:17

Inu Ambuye, Mulungu wathu, mutikomere mtima, ndi kudalitsa zonse zimene timachita, ndithu mudalitse ntchito zonse za manja athu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:4

Mau a munthu angathe kukhala kasupe wa nzeru, ozama ngati nyanja yamchere yaikulu, omweka ngati a mu mtsinje wothamanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:24

Munthu wanzeru amaika mtima pa nzeru, koma chitsiru chimangoti maso mwalamwala pa dziko lonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:9

Mau anga ngoona kwa munthu womvetsa, ngokhoza kwa anthu odziŵa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:11

Munthu wonyoza akalangidwa, wopusapusa amaphunzirapo nzeru. Munthu wanzeru akamlangiza, amamvetsa zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:15

Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma wochenjera amayang'ana m'mene akuyendera.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:30

Palibe nzeru, palibe kumvetsa zinthu, palibe ngakhale uphungu, zimene zingathe kupambana Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 36:9

Kwa Inu kuli kasupe wamoyodi, m'kuŵala kwanu ifenso timaona kuŵala.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 28:20-21

“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Nkuti kumene tingapeze luntha?

Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisikanso kwa mbalame zamumlengalenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:17

Anthu ondikonda, ine nzeru ndimaŵakonda, anthu ondifunafuna mosamala, amandipeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:1-2

Mwana wanga, usaiŵale malangizo angaŵa, koma mtima wako usunge malamulo anga.

Ukatero, nkhokwe zako zidzadzaza ndi dzinthu dzambiri, mbiya zako zidzachita kusefukira ndi vinyo.

Mwana wanga, usanyoze malango a Chauta, usatope nako kudzudzula kwake.

Paja Chauta amadzudzula yemwe amamkonda, monga momwe atate amamchitira mwana wokondwera naye.

Ngwodala munthu amene wapeza nzeru, amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,

pakuti phindu la nzeru nloposa phindu la siliva, nloposanso ndi phindu la golide lomwe.

Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali. Palibe chinthu chochilakalaka cholingana ndi nzeruyo.

Ndi nzeru imene imakupatsa moyo wautali. Ndi nzeru imene imakuninkha chuma ndi ulemu.

Nzeru imakudzeretsa m'njira za chisangalalo, nimakuyendetsa mumtendere mokhamokha.

Nzeru ili ngati mtengo woŵapatsa moyo oigwiritsa. Ngodala amene amaikangamira molimbika.

Pamene adakhazikitsa dziko lapansi, Chauta adaonetsa nzeru. Pamene adakhazikitsa zakumwamba, adaonetsa nzeru za kumvetsa bwino.

Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka, ndipo udzakhala ndi moyo wabwino kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:32-34

“Ndipo tsopano, ana anga, tamverani, ngodala anthu amene amasunga malangizo anga.

Muzimva malangizo, kuti muzikhala anzeru, musamanyozere mau anga.

Ngwodala munthu amene amatchera khutu kwa ine, amene amakhala pakhomo panga tsiku ndi tsiku, amene amadikira pa chitseko changa.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:28

Khristuyo ndiye amene timamlalika. Timachenjeza ndi kuphunzitsa munthu aliyense ndi nzeru zonse zimene tili nazo. Pakuti tikufuna kusandutsa munthu aliyense kuti akhale wangwiro mwa Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:5

Munthu wanzeru ndi wamphamvu kupambana munthu wa nyonga zambiri, munthu wophunzira amaposa munthu wamphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 4:15-16

Ntchito zimenezi uzizichita mosamala ndi modzipereka, kuti anthu onse aone kuti moyo wako wautumiki ukukulirakulira.

Udziyang'anire bwino wekha, ndi kusamala zimene umaphunzitsa. Ulimbikire kutero, chifukwa pakuchita zimenezi udzadzipulumutsa iwe wemwe, ndiponso anthu amene amamva mau ako.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 12:13-14

Basi, zonse zamveka. Mfundo yeniyeni ya zonsezi ndi iyi: Uzimvera Mulungu, ndipo uzitsata malamulo ake, pakuti umenewu ndiwo udindo wake wonse wa munthu.

Pajatu Mulungu adzaweruza zonse zimene timachita, zabwino kapena zoipa, ngakhale ndi zam'chinsinsi zomwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 9:8-9

Wonyoza usamdzudzule, angadane nawe. Koma ukadzudzula munthu wanzeru, adzakukonda.

Wanzeru ukamlangiza, adzakhala wanzeru koposa. Munthu wochita chilungamo ukamuphunzitsa, adzadziŵa zambiri koposa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:33

Nzeru zimakhala mumtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma mumtima mwa zitsiru sizipezeka.

Mutu    |  Mabaibulo