Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

149 Mau a Mulungu Odziwa Zonse


Masalimo 139:1-4

Chauta mwafufuzafufuza, ndipo mwandidziŵa.

ngakhale kumenekonso mudzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandichirikiza.

Ndikanena kuti, “Mdima undiphimbe, kuŵala kumene kwandizinga kusanduke mdima,”

ngakhale mdimawo, kwa Inu si mdima konse, kwa Inu usiku umaŵala ngati usana, mdima uli ngati kuŵala.

Paja ndinu mudapanga za m'kati mwanga, mudandiwumba m'mimba mwa amai anga.

Ndikukutamandani, Inu oopsa ndi odabwitsa. Ntchito zanu zonse nzodabwitsa. Mumandidziŵa bwino kwambiri.

Mapangidwe anga sadabisike pamaso panu pamene ndinkapangidwa mwachinsinsi, pamene ndinkaumbidwa mwaluso m'mimba mwa amai anga.

Maso anu adandiwona ndisanabadwe. Masiku a moyo wanga mudaŵalemberatu m'buku mwanu, asanayambe nkuŵerengedwa komwe.

Maganizo anu, Inu Mulungu, ndi ozama kwa ine, ndi osaŵerengeka konse.

Ndikadaŵaŵerenga, bwenzi ali ambiri koposa mchenga. Ndikamadzuka ndimakhala nanube.

Ndikadakonda kuti muwononge anthu oipa, Inu Mulungu, ndipo kuti anthu okhetsa magazi andichokere.

Inu mumadziŵa pamene ndikhala pansi, pamenenso ndidzuka, mumazindikira maganizo anga muli kutali.

Anthuwo amakunenani zinthu zoipa, namakuukirani ndi mtima woipa.

Kodi sindidana nawo anthu odana nanu, Inu Chauta? Kodi sindinyansidwa nawo anthu okuukirani?

Ndimadana nawo ndi chidani chenicheni. Ndimaŵayesa adani anga.

Fufuzeni, Inu Mulungu, kuti mudziŵe mtima wanga. Yeseni kuti mudziŵe maganizo anga.

Muwone ngati ndimatsata njira yoipa iliyonse, ndipo munditsogolere m'njira yanu yamuyaya.

Mumandipenyetsetsa ndikamayenda ndiponso ndikamagona, mumadziŵa njira zanga zonse.

Ngakhale mau anga asanafike pakamwa panga, Inu Chauta mumaŵadziŵa onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:13

Pamaso pa Mulungu palibe kanthu kobisika, zonse zili poyera ndipo nzovundukuka pamaso pa Iye amene tiyenera kumufotokozera zonse zimene tachita.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:20

nthaŵi zonse pamene mtima wathu ukutitsutsa kuti ndife olakwa. Paja Mulungu ndi wamkulu kopambana mtima wathu, ndipo amadziŵa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:28

Kodi sudziŵa? Kodi sudamve? Chauta ndiye Mulungu wachikhalire, Mlengi wa dziko lonse lapansi. Satopa kapena kufooka, palibe amene amadziŵa maganizo ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:3

Maso a Chauta ali ponseponse, amayang'ana oipa ndi abwino omwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:5

Mbuye wathu ndi wamkulu, ndipo ndi wa mphamvu zambiri, nzeru zake nzopanda malire.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 11:33-34

Chuma cha Mulungu nchachikulu zedi. Nzeru zake ndi kudziŵa kwake nzozama kwambiri. Ndani angamvetse maweruzidwe ake, ndipo njira zake ndani angazitulukire?

Ndi monga mau a Mulungu anenera kuti, “Ndani amadziŵa maganizo a Chauta, ndani angamupatse malangizo?

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 1:5

“Ndisanakulenge m'mimba mwa mai wako, ndinali nditakudziŵa kale. Usanabadwe nkomwe, ndinali ntakupatula kale, ndidakuika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 37:16

Kaya mukudziŵa m'mene Mulungu amayalira mitambo, ntchito yosonyeza nzeru zake zodabwitsa,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 5:21

Mayendedwe a munthu Chauta amaŵaona bwino lomwe, njira zake zonse amazipenyetsetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:30

Inuyotu ngakhale tsitsi lomwe la kumutu kwanu adaliŵerenga lonse.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 28:9

“Ndipo iwe Solomoni mwana wanga, uzimvera Mulungu wa atate ako, ndipo uzimtumikira ndi mtima wonse, modzipereka kwathunthu. Paja Chauta amasanthula mtima wa munthu aliyense, ndipo amadziŵa maganizo a munthu aliyense. Ukamfunafuna, udzampeza. Koma ukalekana naye, Iyeyo adzakutaya mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 94:11

Chauta amadziŵa maganizo a anthu kuti ndi mpweya chabe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 23:24

Kodi munthu nkubisala pobisika potani, pamene Ine sindingathe kumuwona? Kodi Ine sindili ponseponse, kumwamba ndi pa dziko lapansi pano?” Akuterotu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 34:21

“Mulungu amapenya njira zonse za anthu, amaona mayendedwe ao onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:13-15

Chauta ali kumwamba, amayang'ana pansi ndi kuwona anthu onse.

Kumene amakhala pa mpando wachifumuko, amapenya anthu onse okhala pa dziko lapansi

Amene amapanga mitima ya anthu onse, ndiye amene amapenya ntchito zao zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 2:10-11

Ifeyo Mulungu adatiwululira zimenezi mwa Mzimu Woyera. Pajatu Mzimuyo amadziŵa zinthu zonse kotheratu, ngakhalenso maganizo ozama a Mulungu.

Kodi za munthu angazidziŵe ndani, osakhala mzimu wa mwiniwake yemweyo umene uli mwa iyeyo? Momwemonso palibe munthu amene angadziŵe za Mulungu, koma Mzimu wa Mulungu Mwini.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:16

Maso anu adandiwona ndisanabadwe. Masiku a moyo wanga mudaŵalemberatu m'buku mwanu, asanayambe nkuŵerengedwa komwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:2

Makhalidwe a munthu amakhala olungama pamaso pa mwiniwakeyo, koma Chauta ndiye amayesa mtima wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 55:8-9

Chauta akunena kuti, “Maganizo anga ndi maganizo anu si amodzimodzi, ndipo zochita zanga ndi zochita zanu si zimodzimodzi.

Monga momwe mlengalenga uliri kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 44:21

kodi Mulungu sakadazipeza zimenezi? Paja Iye amadziŵa zinsinsi zonse zamumtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:27

Ndipo Mulungu amene amayang'ana za m'kati mwa mitima ya anthu, amadziŵa zimene Mzimu Woyera afuna, pakuti Mzimuyo amapempherera anthu a Mulungu monga momwe Mulungu afunira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 17:10

“Koma Ine Chauta ndimafufuza maganizo ndi kuuyesa mtimawo. Ndimamchitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndiponso moyenerera ntchito zake.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:2

Inu mumadziŵa pamene ndikhala pansi, pamenenso ndidzuka, mumazindikira maganizo anga muli kutali.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:4

Amadziŵa chiŵerengero cha nyenyezi, zonse amazitcha maina ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:8

Inu musamatero ai, pakuti Atate anu amadziŵa zimene mukusoŵa, inu musanapemphe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 21:22

Kodi alipo wina woti angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iyeyo amaweruza ngakhale anthu apamwamba?

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 2:24-25

Koma Yesu sadaikepo chikhulupiriro pa iwowo, popeza kuti Iye ankaŵadziŵa anthu onse.

Sankalira kuti wina achite chomuuza za munthu aliyense. Pakuti mwiniwakeyo ankadziŵa za m'mitima mwa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 3:20

Penanso Malembo akuti, “Ambuye amaŵadziŵa maganizo a anthu anzeru kuti ndi achabe.”

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:12-13

Paja mau a Mulungu ndi amoyo ndi ogwira ntchito mwamphamvu. Ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse. Amabaya mpaka molumikizirana mwa moyo ndi mzimu, ndiponso molumikizirana mfundo ndi mafuta a m'mafupa. Amaweruza ngakhale zimene anthu amalingalira ndi kulakalaka m'mitima mwao.

Pamaso pa Mulungu palibe kanthu kobisika, zonse zili poyera ndipo nzovundukuka pamaso pa Iye amene tiyenera kumufotokozera zonse zimene tachita.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:12

ngakhale mdimawo, kwa Inu si mdima konse, kwa Inu usiku umaŵala ngati usana, mdima uli ngati kuŵala.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:13-14

Ndani adalamulirapo maganizo a Chauta? Ndani adamphunzitsapo kanthu ngati mlangizi wake?

Kodi Chauta adapemphapo nzeru kwa yani, kuti adziŵe zinthu? Ndani adamuphunzitsa kuweruza molungama? Ndani adamphunzitsa kudziŵa zinthu? Ndani adamlangiza njira ya kumvetsa zinthu?

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mafumu 19:27

“Koma Ine ndimadziŵa zonse za iwe, pamene ukhala pansi, pamene uyenda kwina ndi kubwerako, ndiponso pamene undikwiyira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 28:24

Paja Iye amayang'ana mpaka ku mathero a dziko lapansi, amaona zonse zimene zili kunsi kwa thambo.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 11:5

Pamenepo Mzimu wa Chauta udandigwira, ndipo udandiwuza kuti, “Unene kuti zimene akunena Chauta ndi izi, akuti, ‘Inu a m'banja la Israele, ndikudziŵa zimene zili mumtima mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:12

Ukanena kuti, “Ife sitidazidziŵe zimenezi,” kodi iye amene amayesa mtima, zimenezi saziwona? Kodi amene amayang'anira moyo wako sazidziŵa? Kodi sadzambwezera munthu potsata ntchito zake?

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 16:17

Maso anga amaona makhalidwe ao onse oipa, ndi osabisika pamaso panga. Palibenso tchimo lililonse limene sindikulidziŵa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:6

Nzeru zimenezi nzopitirira nzeru zanga, nzapamwamba, sindingathe kuzimvetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 90:8

Inu mwaika machimo athu pamaso panu, ngakhale machimo obisika mwaŵaonetsa poyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:19-20

Pamene adakhazikitsa dziko lapansi, Chauta adaonetsa nzeru. Pamene adakhazikitsa zakumwamba, adaonetsa nzeru za kumvetsa bwino.

Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka, ndipo udzakhala ndi moyo wabwino kwambiri.

Pamene adatumphutsa madzi kuchoka kunsi kwa dziko, ndipo mitambo idagwetsa mvula, adaonetsa nzeru zodziŵa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 2:3

Anthu inu musalankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zodzikuza. Pakuti Chauta ndi Mulungu wanzeru, ndiye amene amaweruza ntchito za anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 11:36

Paja zinthu zonse nzochokera kwa Iye, nzolengedwa ndi Iye ndipo zimalinga kwa Iye. Ulemerero ukhale wake mpaka muyaya. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 50:11

Mbalame zonse zamumlengalenga, zamoyo zonse zoyenda ku thengo ndi zanga.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:11-12

Muzidalira Chauta ndi mphamvu zake. Muziyesetsa kukhala pamaso pake kosalekeza.

Muzikumbukira ntchito zodabwitsa za Chauta, zozizwitsa zimene adachita, ndi m'mene ankaweruzira anthu,

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 34:22

Palibe usiku kapena mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoipa angathe kubisalira Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 12:2

Kanthu kalikonse kovundikirika kadzaululuka, ndipo kalikonse kobisika kadzadziŵika.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 29:15

Tsoka kwa amene amabisira Chauta maganizo ao, amene amachita ntchito zao mu mdima, namaganiza kuti palibe amene akuŵaona ndi kudziŵa zimene akuchita.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:7

Ndidzapita kuti, pofuna kupewa Mzimu wanu, kapena pofuna kuthaŵa nkhope yanu?

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 8:39

pamenepo Inuyo mumve kumwambako kumene mumakhala. Mukhululuke, ndipo muchitepo kanthu. Mumchitire aliyense potsata makhalidwe ake onse, pakuti Inu mukudziŵa mtima wake. Inu nokha ndinu amene mumadziŵa mitima ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mbiri 16:9

Paja maso a Chauta amayang'ana uku ndi uku pa dziko lonse lapansi, kuti aonetse mphamvu zake kwa anthu amene mtima wao uli wangwiro kwa Iyeyo. Inuyo mwachita zopusa pa zimenezi. Ndiye kuyambira tsopano lino, mpaka m'tsogolo muno, mudzakhala pa nkhondo.”

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 1:2

Mulungu Atate adakusankhani, monga Iye adaziganiziratu kuyambira pa chiyambi, kuti Mzimu Woyera akuyeretseni ndipo kuti mumvere Yesu Khristu, ndi kutsukidwa ndi magazi ake. Mulungu akukomereni mtima ndi kukupatsani mtendere wonka nuchulukirachulukira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:15

Akapereka lamulo pa dziko lapansi, mau ake amayenda mwaliŵiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 15:18

Akutero ndi Chauta amene adaulula zimenezi kuyambira kalekale.’

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:168

Ndimatsata malamulo anu ndi malangizo anu, pakuti makhalidwe anga onse mukuŵaona.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 66:18

“Ndikudziŵa ntchito zao ndi maganizo ao. Ndikubwera kudzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndi a zilankhulo zonse. Adzabweradi ndipo adzaona ulemerero wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 21:17

Yesu adamufunsa kachitatu kuti, “Iwe Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikonda?” Petro adayamba kumva chisoni kuti Yesu akumufunsa kachitatu kuti, “Kodi umandikonda?” Ndipo adati, “Ambuye, mumadziŵa zonse. Mukudziŵa kuti ineyo ndimakukondani.” Yesu adamuuza kuti, “Samala nkhosa zanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 48:6

“Zonsezi udazimva, tsono uzilingalire bwino. Monga iweyo sungazivomereze? Kuyambira tsopano mpaka m'tsogolo muno ndidzakuuza zinthu zatsopano, zinthu zobisika zimene sudazidziŵe konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:24

Mayendedwe a munthu amaŵalamula ndi Chauta: Tsono munthu angadziŵe bwanji njira yake?

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 23:10

Komabe Mulungu amadziŵa m'mene ndimayendera, akandiyesa adzapeza kuti ndine wangwiro ngati golide.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 94:9

Kodi amene adalenga makutu, sangathe kumva? Kodi amene adapanga maso, sangathe kupenya?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:1

Chauta mwafufuzafufuza, ndipo mwandidziŵa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:13

Tikudziŵa kuti timakhala mwa Mulungu, ndipo Iyenso amakhala mwa ife, chifukwa adatipatsa Mzimu wake Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:3

Mumandipenyetsetsa ndikamayenda ndiponso ndikamagona, mumadziŵa njira zanga zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 8:27

“Kodi Mulungu angakhale nawodi pa dziko lapansi? Onani, kumwamba ndi kumwambamwamba komwe sikukukwanirani kukhala, nanji tsono nyumba imene ndakumangiraniyi!

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 2:19

Komabe maziko olimba, amene Mulungu adaŵaika, ngokhazikika, ndipo mau olembedwapo ndi aŵa: “Ambuye amadziŵa amene ali ao”, ndiponso, “Aliyense wotamanda dzina la Ambuye, asiye zosalungama.”

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 17:26-27

Kochokera mwa kholo limodzi Iye adalenga mitundu yonse ya anthu, kuti ikhale pa dziko lonse lapansi. Adakonzeratu nthaŵi ya moyo wao, ndiponso malire a pokhala pao.

Mulungu adafuna kuti anthu amufunefune, ndipo kuti pomfufuzafufuza, mwina nkumupeza. Komabe Iye sali kutali ndi aliyense mwa ife.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:2-3

Chauta akumanga Yerusalemu, akusonkhanitsa Aisraele omwazika.

Sadachitepo zimenezi ndi mtundu wina uliwonse wa anthu, iwo sadziŵa malangizo ake. Tamandani Chauta!

Akuchiritsa a mtima wachisoni, ndipo akumanga mabala ao.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 3:20

Ulemerero ukhale kwa Mulungu amene, mwa mphamvu yake yogwira ntchito mwa ife, angathe kuchita zochuluka kupitirira kutalitali zimene tingazipemphe kapena kuziganiza.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 11:2

Mzimu wa Chauta udzakhala pa Iye, mzimu wopatsa nzeru ndi kumvetsa, mzimu wopatsa uphungu ndi mphamvu, mzimu wopatsa kudziŵa zinthu ndi kuwopa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 16:27

Kwa Mulungu, amene ndiye yekha wanzeru, kukhale ulemerero mwa Yesu Khristu mpaka muyaya. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 44:20-21

Tikadaiŵala Mulungu wathu, kapena kugwadira mulungu wachilendo,

kodi Mulungu sakadazipeza zimenezi? Paja Iye amadziŵa zinsinsi zonse zamumtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:11

Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika kwa Mulungu, nanji tsono mitima ya anthu!

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 45:21

Kambani, fotokozani mlandu wanu. Mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani adaneneratu zimene zidzachitika? Ndani adaloseratu kalekale zimenezo? Kodi si Ineyo, Chautane? Ndithu, kupatula Ine palibe Mulungu wina, Mulungu wachilungamo ndi wopulumutsa. Palibenso wina aliyense kupatula Ine.”

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:8-9

zimene Mulungu adatipatsa mochuluka.

Mwa luntha ndi nzeru adatiwululira chifuniro chake chimene kale chinali chobisika. Zimene adaati achite mwa kukoma mtima kwake ndi zomwe Iye mwini adaakonzeratu kale.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 18:30

Mulungu wathuyo, zochita zake nzangwiro, mau ake sapita pachabe, Iye ndiye chishango choteteza onse othaŵira kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 22:31

Mulungu wathuyo zochita zake nzangwiro, mau a Chauta ndi oona. Iye ndiye chishango choteteza onse othaŵira kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:66

Patseni luntha ndi nzeru, chifukwa ndimakhulupirira malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 38:4-5

“Kodi udaali kuti pamene ndinkaika maziko a dziko lapansi? Undiwuze ngati ndiwe womvetsa zinthu.

pamene ili khale m'mapanga mwake, kapena pamene ikubisala m'tchire?

Kodi khwangwala amampatsa chakudya chake ndani, pamene maunda ake akulirira kwa Mulungu, namadzandira chifukwa chosoŵa chakudya?”

Nanga kodi ukudziŵa amene adalemba malire ake, amene adayesapo ndi chingwe padzikopo?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:15

Mapangidwe anga sadabisike pamaso panu pamene ndinkapangidwa mwachinsinsi, pamene ndinkaumbidwa mwaluso m'mimba mwa amai anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:26

Yang'anani kumlengalenga. Kodi ndani adalenga nyenyezi mukuziwonazi? Ndiye amene amazitsogolera ngati gulu lankhondo, ndipo iliyonse amaiitana ndi dzina lake. Popeza kuti nyonga ndi mphamvu zake nzazikulu. Palibe ndi imodzi yomwe imene imasoŵapo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:12

Paja Ambuye amaŵayang'anira bwino anthu olungama amatchera khutu ku mapemphero ao. Koma ochita zoipa saŵayang'ana bwino.”

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 9:4

Koma Yesu adaadziŵa zimene iwo ankaganiza, motero adaŵafunsa kuti, “Bwanji mukuganiza zoipa mumtima mwanu?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:1

Tamandani Chauta! Nkwabwino kuimba nyimbo zotamanda Mulungu wathu, nkokondwetsa mtima kumtamanda moyenera.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 1:25

Pajatu chimene chimaoneka ngati kupusa kwa Mulungu, nchanzeru kupambana nzeru za anthu. Ndipo chimene chimaoneka ngati kufooka kwa Mulungu, nchamphamvu kupambana mphamvu za anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:14

Kodi Chauta adapemphapo nzeru kwa yani, kuti adziŵe zinthu? Ndani adamuphunzitsa kuweruza molungama? Ndani adamphunzitsa kudziŵa zinthu? Ndani adamlangiza njira ya kumvetsa zinthu?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:7

Adzasimba za ubwino wanu, adzaimba nyimbo zotamanda kulungama kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 3:9

Adandipatsanso ntchito yofotokozera anthu onse za m'mene Mulungu adzachitira zonse zimene Iye adakonzeratu mwa chinsinsi chake. Mulungu amene adalenga zonse, adasunga chinsinsichi chikhalire, nthaŵi isanayambe.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 2:3

Mwa Iyeyu mudzapeza chuma chonse chobisika, ndiye kuti nzeru ndi luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 12:13

“Koma Mulungu ali ndi nzeru ndi mphamvu zopambana. Ali ndi uphungu wabwino, ndi kumvetsa zinthu zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 104:24

Inu Chauta ntchito zanu nzambiri, zonse mwazipanga mwanzeru, ndipo dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 55:9

Monga momwe mlengalenga uliri kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 38:1-2

Apo Chauta adayankha Yobe m'kamvulumvulu kuti,

Ndidailembera malire, ndidaiikira mipiringidzo ndi zitseko zake.

Tsono ndidati, ‘Ufike mpaka apo osabzolapo, mafunde ako amphamvuwo aime pomwepo.’

“Kodi chibadwire chako udalamulapo dzuŵa kuti lituluke m'maŵa, ndi kuti mbandakucha ukhalepo pa nthaŵi yake?

Kodi iweyo udalamulapo kuti kuŵala kwa mbandakuchawo kuunikire dziko lonse lapansi, kuti kuthaŵitse anthu oipa obisala pamenepo?

Chifukwa cha kuŵala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala ngati zilembo za chidindo pa mtapo.

Kuŵala kwa dzuŵa sikuŵafika anthu oipa, choncho sangathe kugwira ntchito zao.

“Kodi udakayendapo pansi penipeni pa nyanja ndi kukafika pa magwero ake?

Kodi adakuwonetsa iwe zipata za imfa? Kodi udaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wokhawokha?

Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziŵa? Undiwuze tsono ngati umazidziŵa zonsezi.

“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuŵala ili kuti? Nanga mdima, kwao nkuti?

“Kodi ndiwe amene ukusokoneza uphungu wanga polankhula mau opanda nzeru?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:14

Amadziŵa m'mene adatipangira, amakumbukira kuti ife ndife fumbi.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 8:17

Pajatu chinthu chilichonse chobisika chidzaululuka, ndipo chilichonse chachinsinsi chidzadziŵika nkuwonekera poyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 46:10

Ndidaneneratu zakumathero kuchokera pa chiyambi pomwe. Kuyambira kalekale ndidaloseratu zimene zidakali zosachitikabe. Ndidaanena kuti, ‘Maganizo anga sadzalephera, ndidzachitadi zonse zimene ndidafuna kuchita.’

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 77:14

Inu ndinu Mulungu amene mumachita zodabwitsa, amene mwaonetsa mphamvu zanu pakati pa mitundu ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 11:33

Chuma cha Mulungu nchachikulu zedi. Nzeru zake ndi kudziŵa kwake nzozama kwambiri. Ndani angamvetse maweruzidwe ake, ndipo njira zake ndani angazitulukire?

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 29:11-12

Inu Ambuye, ndinu aakulu, amphamvu, aulemerero, opambana pa nkhondo ndiponso oposa pa ulemu, pakuti zonse zakumwamba ndi za pansi pano nzanu. Mfumu ndinu nokha, Inu Chauta, ndipo wolamulira zonse ndinu.

Chuma ndi ulemu zimachokera kwa Inu ndipo mumalamulira zonse, chifukwa muli ndi mphamvu zonse. Inu nokha mutha kukweza munthu ndi kumpatsa mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 9:10

Kulemekeza Chauta ndiye chiyambi cha nzeru, kudziŵa Woyera uja nkukhala womvetsa bwino zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:142

Kulungama kwanu nkwamuyaya, ndipo malamulo anu ndi oona.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 50:4

Ambuye Chauta andiphunzitsa zoyenera kunena, kuti ndidziŵe mau olimbitsa mtima anthu ofooka. M'maŵa mulimonse amandidzutsa, amathwetsa makutu anga kuti ndimve, monga amachitira amene akuphunzira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 42:9

Zinthu zimene ndidalosa zija zachitikadi. Tsono ndikuuzani zinthu zatsopano, zisanaoneke ndikukudziŵitsiranitu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:26

Mauwo ndi chinsinsi chozama chimene chinali chobisika chikhalire kwa mibadwo yonse, koma tsopano Mulungu wachiwululira anthu ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 26:14

Zimenezi ndi pang'ono chabe za makhalidwe ake. Tingomva pang'ono za Iye ngati kunong'ona. Koma ndani angadziŵe kukula kwa mphamvu zake?”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 11:3

Ndipo kuwopa Chauta ndiye chidzakhale chinthu chomkondweretsa. Sadzaweruza potsata zooneka pamaso, kapena kugamula mlandu potsata zakumva.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:29

Pakuti anthu amene Mulungu adaŵasankhiratu, Iye adaŵapatulanso kale kuti akhale monga Mwana wake, kuti choncho Mwanayo akhale woyamba mwa abale ambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:3

Chauta ndi wamkulu ndi woyenera kumtamanda kwambiri, ndipo ukulu wake sitingathe kuumvetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 1:17

Kwa Mfumu yamuyaya, yosafa, yosaoneka, amene Iye yekha ndiye Mulungu, kukhale ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 29:29

Pali zinthu zina zimene Chauta, Mulungu wathu, sanatiululire; koma watiululira ifeyo ndi zidzukulu zathu malamulo ake amene tiyenera kuwamvera nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 111:10

Kuwopa Chauta ndiye chiyambi cha nzeru. Wotsata malamulo ake amakhala ndi nzeru zenizeni. Chauta ndi wotamandika mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:15

Sitili ndi Mkulu wa ansembe woti sangathe kutimvera chifundo chifukwa cha zofooka zathu. Wathu Mkulu wa ansembe onse adayesedwa pa zonse, monga momwe ife timayesedwera, koma Iye sadachimwe konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:12

Kodi ndani adayesa kuchuluka kwa madzi am'nyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyesa kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani adayesa dothi lonse la dziko lapansi ndi dengu? Ndani adayesa kulemera kwa mapiri ndi magomo pa sikelo?

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 11:7-9

“Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungathe kudziŵa kukula kwa nzeru za Mphambe?

Malire a nzeru zake ali kutali kuposa mlengalenga. Nanga iwe ungachitepo chiyani? Malire a nzeru zake ndi ozama kupitirira dziko la anthu akufa. Nanga iwe ungathe kudziŵapo chiyani?

Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana kutalika kwa dziko lapansi, ndi kupingasa kwa nyanja zamchere.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 8:2-3

Munthu amene amadziyesa wodziŵa kanthu, ndiye kuti sakudziŵabe kwenikweni monga momwe akadayenera kudziŵira.

Koma munthu akamakonda Mulungu, ndiye kuti amadziŵika ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:73

Manja anu adandilenga ndi kundiwumba. Patseni nzeru zomvetsa, kuti ndiziphunzira malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 38:16

“Kodi udakayendapo pansi penipeni pa nyanja ndi kukafika pa magwero ake?

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:1

Zolinga zamumtima ndi za munthu, koma zolankhula zake ndi zochokera kwa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 42:8-9

Ine ndine Chauta, dzina langa nlimenelo. Ulemerero wanga sindidzapatsa wina aliyense. Mayamiko oyenera Ine, sindidzalola kuti mafano alandireko.

Zinthu zimene ndidalosa zija zachitikadi. Tsono ndikuuzani zinthu zatsopano, zisanaoneke ndikukudziŵitsiranitu.”

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 2:6-7

Komabe pakati pa anthu okhwima m'chikhulupiriro, timalankhula zanzeru. Koma nzeruzo si za masiku anozi, kapena za akulu olamulira dziko lino lapansi, amene mphamvu zao nzodzatha.

Nzeru zimene timalankhula, ndi nzeru za Mulungu, zachinsinsi, zobisika kwa anthu. Mulungu asanalenge dziko lapansi, adaakonzeratu zimenezi kuti atipatse ulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 32:8

Chauta akuti, “Ndidzakudziŵitsa ndi kukuphunzitsa njira imene uyenera kuyendamo. Ndidzakulangiza ndi kukuyang'anira.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:26-27

Momwemonso Mzimu Woyera amatithandiza. Ndife ofooka, osadziŵa m'mene tiyenera kupempherera. Nchifukwa chake Mzimu Woyera mwiniwake amatipempherera ndi madandaulo osafotokozeka.

Ndipo Mulungu amene amayang'ana za m'kati mwa mitima ya anthu, amadziŵa zimene Mzimu Woyera afuna, pakuti Mzimuyo amapempherera anthu a Mulungu monga momwe Mulungu afunira.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 13:12

Tsopano timaona zinthu ngati m'galasi, zosaoneka bwino kwenikweni. Koma pa nthaŵiyo tidzaona chamaso ndithu. Tsopano ndimangodziŵa mopereŵera, koma pa nthaŵiyo ndidzamvetsa kotheratu, monga momwe Mulungu akundidziŵira ine kotheratu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 66:1-2

Chauta akunena kuti, “Thambo lam'mwamba ndiye mpando wanga waufumu, dziko lapansi ndiye chopondapo mapazi anga. Kodi ndi nyumba yotani imene mungathe kundimangira inu? Ndi malo otani amene inu mungandikonzere kuti Ine ndizipumulirapo?

“Kondwera nayeni Yerusalemu, musangalale chifukwa cha iye, inu nonse amene mumakonda mzinda umenewu. Kondwera nayeni mwachimwemwe, nonsenu amene mukumlira.

Mudzalandira chitonthozo ndi kukondwera nacho kwambiri. Mudzagaŵana naye ulemerero wake ndi kusangalala nawo.”

Chauta akunena kuti, “Ndidzakupatsa zabwino zochuluka ngati mtsinje wa madzi. Chuma cha mitundu ya anthu chidzafika kwa inu ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene mai wake wamnyamulira pambalipa, kapena akumluluza pa maondo.

Ndidzakusangalatsani ku Yerusalemu monga momwe mai amasangalatsira mwana wake.

Mudzasangalala poona zimenezi. Zidzakulimbitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Tsono mudzadziŵa kuti Ine Chauta ndimathandiza amene amandimvera, ndipo ndimakwiyira adani anga.”

“Pajatu Chauta adzabwera ndi moto. Ndipo magaleta ake adzafika ngati mkuntho. Iye adzaonetsa poyera ukali wake, ndipo adzalanga adani ake ndi malaŵi a moto.

Adzalanga anthu onse a pa dziko lapansi ndi moto ndi lupanga. Alipo ambiri amene Chauta adzaŵapha.”

Chauta akunena kuti, “Amene akuti akudzipatula ndi kudziyeretsa pamene akufuna kuchita miyambo yam'minda ija, ali ndi mtsogoleri wao yemwe, nkumadya nyama yankhumba, mbeŵa ndi zonyansa zina, onsewo adzafera limodzi,” akuterotu Chauta.

“Ndikudziŵa ntchito zao ndi maganizo ao. Ndikubwera kudzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndi a zilankhulo zonse. Adzabweradi ndipo adzaona ulemerero wanga.

“Ndidzaika chizindikiro pakati pao. Mwa iwowo padzakhala ena opulumukako amene ndidzaŵatuma kwa anthu a mitundu ina, monga a ku Tarisisi, a ku Puti ndi a ku Ludi, akatswiri a mauta, ndiponso ku Tubala, ku Yavani, ndi ku maiko akutali amene sadamvepo za mbiri yanga kapena kuwona ulemerero wanga. Iwowo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.

Zinthu zonsezi ndidazilenga ndine, tsono zonsezi nzanga,” akutero Chauta. “Anthu amene ndimakondwera nawo ndi aŵa: odzichepetsa ndi olapa, ondiwopa ndi omvera mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 12:10

M'manja mwake ndimo muli zamoyo zonse, mulinso moyo wa anthu a mitundu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:18

Ndimapemphera kuti Mzimu Woyerayo akuunikireni m'mitima mwanu, kuti mudziŵe zimene mungathe kuyembekezera kwa Mulungu amene adakuitanani. Ndimafunanso kuti mudziŵe kukula kwake kwa ulemerero ndi madalitso amene Mulungu amalonjeza kupatsa anthu ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 56:8

Inu mwaona kupiripita kwanga, mudziŵa kuchuluka kwa misozi yanga. Kodi zonsezi sizidalembedwe m'buku lanu?

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 16:7

Koma Chauta adauza Samuele kuti, “Usayang'ane maonekedwe ake, ngakhale kutalika kwa msinkhu wake, poti ndamkana ameneyo. Chauta sapenya monga m'mene apenyera anthu. Anthu amapenya zakunja, koma Chauta amapenya zamumtima.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 5:3

Kodi Inu Chauta, suja mumafuna anthu onena zoona? Inu mudaŵakantha anthuwo, koma iwo sadamve kuŵaŵa. Mudaŵatswanya, koma sadafune kutembenuka mtima. Adaumitsa mitima yao ngati mwala, adakana kwamtuwagalu kulapa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:9

Mtima wa munthu umalingalira zoti uchite, koma Chauta ndiye amene amaongolera mayendedwe a munthuyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 11:3

Pokhala ndi chikhulupiriro timamvetsa kuti zonse zimene zilipo zidalengedwa ndi mau a Mulungu, mwakuti zinthu zoonekazi zidachokera ku zinthu zosaoneka.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 28:29

Nzeru zimenezi zimachokera kwa Chauta Wamphamvuzonse. Uphungu wake ndi wodabwitsa, nzeru zake nzopambana.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 12:22

Amavundukula zamumdima, ndipo mdimawo amausandutsa kuŵala.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 2:16

Monga unenera Uthenga Wabwino umene ndimalalika, zidzateronso pa tsiku lija limene Mulungu mwa Khristu Yesu adzaweruza zinsinsi za m'mitima mwa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 11:27

“Atate adaika zonse m'manja mwanga. Palibe wina wodziŵa Mwana kupatula Atate okha. Palibenso wina wodziŵa Atate kupatula Mwana yekha, ndiponso amene Mwanayo akufuna kumuululira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 28:12

“Koma nzeru zingapezeke kuti? Luntha lingapezeke kuti?

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:7

Usamadziwona ngati wanzeru. Uziwopa Chauta, ndipo uleke zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:14

Chauta amapalana chibwenzi ndi anthu omvera Iye, ndipo amaŵadziŵitsa chipangano chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 12:6-7

“Suja amagulitsa atimba asanu tindalama tiŵiri? Komabe Mulungu saiŵala ndi mmodzi yemwe.

Ndipo tsitsi lomwe la kumutu kwanu adaliŵerenga lonse. Choncho musati muziwopa ai. Ndinu a mtengo woposa atimba ambiri.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:30

Palibe nzeru, palibe kumvetsa zinthu, palibe ngakhale uphungu, zimene zingathe kupambana Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 9:11

Ngakhale anawo asanabadwe, ndiye kuti tsono asanachite chilichonse chabwino kapena choipa, Mulungu adaafunabe kuti cholinga chake chosankhira munthu aliyense chipitirire. Izi adachita osati chifukwa cha ntchito za munthu koma chifukwa chakuti Mulungu adamuitana munthuyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 36:9

Kwa Inu kuli kasupe wamoyodi, m'kuŵala kwanu ifenso timaona kuŵala.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 8:4

ndimadzifunsa kuti, “Kodi munthu nchiyani kuti muzimkumbukira, mwana wa munthu nchiyani kuti muzimsamalira?”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 14:24

Chauta Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Monga momwe ndaganizira, zidzachitikadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 3:8

Koma inu okondedwa, chinthu chimodzi musaiŵale, kuti pamaso pa Ambuye tsiku limodzi lili ngati zaka chikwi chimodzi, ndipo zaka chikwi chimodzi zili ngati tsiku limodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 4:5

Motero musaweruziretu munthu aliyense, Ambuye asanabwere. Iwo ndiwo adzaunika pa zonse zobisika mu mdima, ndipo adzaulula maganizo a m'mitima mwa anthu. Pamenepo aliyense adzalandira kwa Mulungu chiyamiko chomuyenerera.

Mutu    |  Mabaibulo