Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

68 Mau a Mulungu: Malemba Opatulika

Mawu a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu. Amandiwongolera pa zochitika zonse za moyo wanga, akundionetsa njira ndikakadzuka, ndi kundipatsa mayankho pamavuto anga. Ndikofunikira osati kungokhulupirira Mawu a Mulungu ngati choonadi chokha, komanso kuwatsatira pa moyo wanga.

Monga mmene Salmo 119:105 imanenera, Mawu ake ndi nyali ya kumapazi anga, ndi kuunika pa njira yanga. Mawu a Mulungu saunikira kokha ulendo wanga, komanso amandidziwitsa chikondi chimene Mulungu ali nacho pa ine.

Ndikofunikira kukumbukira kuti si chinthu cha kanthawi kochepa, koma monga taonera kale, Mawu a Mulungu amakhala kosatha.


Yohane 8:31-32

Yesu adauza anthu amene adamkhulupirirawo kuti, “Ngati mumvera mau anga nthaŵi zonse, ndiye kuti ndinudi ophunzira anga.

Mudzadziŵa zoona zenizeni, ndipo zoonazo zidzakusandutsani aufulu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:20-21

Mwana wanga, mvetsetsa mau anga. Tchera khutu ku zimene ndikunena.

Zisachoke m'mutu mwakomu, uzisunge bwino mumtima mwako.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:16

Mau a Khristu akhazikike kwathunthu m'mitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana ndi nzeru zonse. Muziimbira Mulungu ndi chiyamiko m'mitima mwanu, pamene mukuimba masalimo, nyimbo zotamanda Mulungu ndi nyimbo zina zauzimu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:160

mau anu ndi oona okhaokha, malangizo anu onse olungama ngamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:11

Ndasunga mau anu mumtima mwanga, kuti ndisakuchimwireni.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 130:5

Ndimayembekeza chithandizo cha Chauta, ndimayembekeza ndi mtima wonse, ndipo ndimakhulupirira mau ake.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 22:31

Mulungu wathuyo zochita zake nzangwiro, mau a Chauta ndi oona. Iye ndiye chishango choteteza onse othaŵira kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 1:23

Pakuti mwa mwachita kubadwanso, moyo wake si wochokera m'mbeu yotha kuwonongeka, koma m'mbeu yosatha kuwonongeka. Mbeuyi ndi mau a Mulungu, mau amoyo ndi okhala mpakampaka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:7

Mau a Chauta ngangwiro, amapatsa munthu moyo watsopano. Umboni wa Chauta ndi wokhulupirika, umaŵapatsa nzeru amene alibe.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 12:28

Tsono uŵauze kuti, Zimene ndikunena Ine Ambuye Chauta ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso ai. Ndidzachitadi chilichonse chimene ndanena. Ndikutero Ine Chauta!”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:5

Usaiŵale mau a pakamwa pangaŵa, usatayane nawo, Ukhale ndi nzeru, ndiponso khalidwe la kumvetsa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:3

Inu mwayera kale chifukwa cha mau amene ndakuuzani.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:18

Ndithu ndikunenetsa kuti thambo ndi dziko lapansi zisanathe, sipadzachoka kalemba nkakang'ono komwe kapena kankhodolera pa Malamulowo, mpaka zonse zitachitika.

Mutu    |  Mabaibulo
Yoswa 1:8

Uziŵerenga buku lamalamuloli, ndipo usana ndi usiku uzisinkhasinkha zolembedwa m'menemo, kuti uzisunge zonse. Tsono ukamatero, udzapeza bwino ndipo udzapambana.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 4:2

Musaonjezerepo kanthu kena pa zimene ndakulamulani, ndipo musachotsepo kanthu. Muzimvera malamulo a Chauta, Mulungu wanu, amene ndakupatsani.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:103

mau anu ndi otsekemera kwambiri ndikaŵalaŵa. Amatsekemera kuposa uchi m'kamwa mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 12:6

Malonjezo a Chauta ndi angwiro, ali ngati siliva womkometsa m'ng'anjo yamoto, woyeretsedwa kasanunkaŵiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:7

Ngati mukhala mwa Ine, ndipo mau anga akhala mwa inu, mupemphe chilichonse chimene mungachifune, ndipo mudzachilandiradi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 55:11

Ndimonso amachitira mau ochokera m'kamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine popanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo zimene ndidaŵatumira zidzayenda bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 15:16

Nditamva mau anu, ndidaŵalandira bwino, mauwo adandipatsa chimwemwe ndi chisangalalo. Paja Inu Chauta Wamphamvuzonse, ndimadziŵika ndi dzina lanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:140-144

Malonjezo anu ndi otsimikizika, ndipo ine mtumiki wanu ndimaŵakonda.

Ine ndine wamng'ono ndi wonyozeka, komabe sindiiŵala malamulo anu.

Kulungama kwanu nkwamuyaya, ndipo malamulo anu ndi oona.

Mavuto andigwera pamodzi ndi zoŵaŵa zomwe, koma malamulo anu amandisangalatsa.

Malamulo anu ndi olungama mpaka muyaya, patseni nzeru zomvetsa kuti ndizikhala ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:12

Paja mau a Mulungu ndi amoyo ndi ogwira ntchito mwamphamvu. Ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse. Amabaya mpaka molumikizirana mwa moyo ndi mzimu, ndiponso molumikizirana mfundo ndi mafuta a m'mafupa. Amaweruza ngakhale zimene anthu amalingalira ndi kulakalaka m'mitima mwao.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 3:16-17

Malembo Oyera onse ndi Mulungu amene adaŵalembetsa mochita ngati kuŵauzira, ndipo amathandiza pakuphunzitsa choona, pakutsutsa zolakwa, pakuwongola zokhota, ndi pakuphunzitsa anthu za kukhala olungama.

Motero Malembo amathandiza munthu wa Mulungu kukhala wokhoza kwenikweni, ndi wokonzekeratu kuchita ntchito yabwino iliyonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:105

mau anu ndiye nyale ya mapazi anga, ndipo amaunikira njira yanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:22

Musamadzinyenga pakungomva chabe mau a Mulungu, koma muzichita zimene mauwo anena.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:17

Landirani chipulumutso ngati chisoti chanu, ndi mau a Mulungu ngati lupanga limene Mzimu Woyera akupatsani.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 11:28

Koma Yesu adati, “Iyai, odala ndi anthu amene amamva mau a Mulungu naŵagwiritsa ntchito.”

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 11:18

Malamulo ameneŵa akhale m'mitima mwanu ndi m'maganizo mwanu. Muŵamange pamikono panu ndi pa mphumi pakati pa maso anu, kuti akhale chikumbutso.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 18:30

Mulungu wathuyo, zochita zake nzangwiro, mau ake sapita pachabe, Iye ndiye chishango choteteza onse othaŵira kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:24

“Munthu aliyense womva mau angaŵa nkumaŵagwiritsa ntchito, amafanafana ndi munthu wanzeru amene adaamanga nyumba yake pa thanthwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 24:35

Thambo ndi dziko lapansi zidzatha, koma mau anga sadzatha mphamvu konse.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:130

Kufotokozera mau anu kumakhala ngati kuŵala, kumapatsa nzeru za kumvetsa kwa anthu opanda nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 4:4

Koma Yesu adati, “Malembo akuti, “ ‘Munthu sangakhale moyo ndi chakudya chokha, koma ndi mau onse olankhula Mulungu.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 5:24

“Ndithu ndikunenetsa kuti munthu womva mau anga, nakhulupirira Iye amene adandituma, ameneyo ali ndi moyo wosatha. Iyeyo sazengedwa mlandu, koma watuluka kale mu imfa, ndipo waloŵa m'moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:4

Mau a Chauta ndi olungama, zochita zake zonse amazichita mokhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 21:33

Thambo ndi dziko lapansi zidzatha, koma mau anga sadzatha mphamvu konse.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:8

Malangizo a Chauta ndi olungama, amasangalatsa mtima. Malamulo a Chauta ndi olungama, amapatsa mtima womvetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:8

Udzu umauma, maluŵa amafota, koma mau a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:9

Kodi mnyamata angathe bwanji kusunga makhalidwe ake kuti akhale angwiro? Akaŵasamala potsata mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:114

Inu ndinu malo anga obisalako ndiponso chishango changa, ndimakhulupirira mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 1:1

Pachiyambi pa zonse Iye amene amatchedwa dzina loti Mau, anali alipo kale. Anali kwa Mulungu, ndipo anali Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 30:5

Mau aliwonse a Mulungu ndi oona. Iye ndiye chishango choteteza amene amathaŵira kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 1:3

Iye ndiye kuŵala koonetsa ulemerero wa Mulungu, ndipo ndiye chithunzi chenicheni chosonyeza khalidwe la Mulungu. Iyeyu amachirikiza zonse ndi mau ake amphamvu. Atayeretsa mtundu wa anthu pakuŵachotsa machimo, adakakhala Kumwamba, ku dzanja lamanja la Mulungu waulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 23:12

Sindidapatuke kusiya malamulo ake. Ndasunga mau a pakamwa pake kupambana zofuna zanga zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:97

Ndimakonda malamulo anu kwambiri, ndimasinkhasinkha za malamulowo tsiku lonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:165

Anthu okonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, palibe china chotha kuŵagwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 1:25

koma mau a Ambuye ngokhala mpaka muyaya.” Mau ameneŵa ndi Uthenga Wabwino umene walalikidwa kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 17:17

Muziŵapatula ndi mau anu kuti akhale anthu anu. Mau anuwo ngoona zedi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 10:17

Motero munthu amakhulupirira chifukwa cha zimene wamva, ndipo zimene wamvazo zimachokera ku zolalika za Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 1:8-9

Koma aliyense, kaya ndife kaya ndi mngelo wochokera Kumwamba, akakulalikirani uthenga wabwino wosiyana ndi uja tidakulalikiraniwu, ameneyo akhale wotembereredwa.

Ndikubwereza kunena zimene tidaanenanso kale, kuti munthu aliyense akakulalikirani uthenga wabwino wosiyana ndi Uthenga Wabwino umene mudalandira uja, iyeyo akhale wotembereredwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:7-8

Mau a Chauta ngangwiro, amapatsa munthu moyo watsopano. Umboni wa Chauta ndi wokhulupirika, umaŵapatsa nzeru amene alibe.

Malangizo a Chauta ndi olungama, amasangalatsa mtima. Malamulo a Chauta ndi olungama, amapatsa mtima womvetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 138:2

Ndikugwada moŵerama kumaso kwa Nyumba yanu yoyera. Ndikutamanda dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika, chifukwanso cha kukhulupirika kwanu. Mwakweza dzina lanu ndiponso malonjezo anu kupambana chinthu china chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 2:13

Pa mbali yathu, timathokoza Mulungu kosalekeza. Timatero chifukwa chakuti pamene mudamva mau a Mulungu amene tidakulalikirani, mudaŵalandira osati ngati mau a anthu chabe, koma monga momwe aliri ndithu, mau a Mulungu. Mauwo ndi omwe akugwira ntchito mwa inu okhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:14

Ndimakulemberani inu ana, chifukwa Atate mumaŵadziŵa. Ndimakulemberani inu atate, chifukwa mumamdziŵa Iye amene alipo kuyambira pa chiyambi. Ndimakulemberani inu achinyamata, chifukwa ndinu amphamvu, mau a Mulungu amakhala mwa inu, ndipo mwampambana Woipa uja.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 1:1-3

Ngwodala munthu wosatsata uphungu wa anthu oipa, wosatsanzira mayendedwe a anthu ochimwa, wosakhala nawo m'gulu la anthu onyoza Mulungu,

koma wokondwerera kumvera malamulo a Chauta, nkumasinkhasinkha za malamulowo usana ndi usiku.

Munthuyo ali ngati mtengo wobzalidwa m'mbali mwa mtsinje wa madzi, ngati mtengo wobereka zipatso pa nthaŵi yake, umene masamba ake safota konse. Zochita zake zonse zimamuyendera bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 6:6-7

Muziŵasunga bwino mumtima mwanu malamulo amene ndikukupatsani leroŵa.

Muziŵaphunzitsa mwachangu kwa ana anu kulikonse kumene muli, mutakhala pansi m'nyumba mwanu, kapena muli paulendo, kapena mukupumula, kapena mukugwira ntchito.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:8-9

Kuthaŵira kwa Chauta nkwabwino kupambana kukhulupirira munthu.

Kuthaŵira kwa Chauta nkwabwino kupambana kukhulupirira mafumu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:6

Paja Chauta ndiye amapatsa nzeru, Iye ndiye kasupe wa kudziŵa zinthu ndi wa kumvetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:5

Koma munthu akamasunga mau a Mulungu, pamenepo chikondi cha Mulungu chafikadi pake penipeni mwa iyeyo. Chotitsimikizitsa kuti tili mwa Iye, ndi chimenechi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:4

Zonse zolembedwa m'Malembo kale, zidalembedwa kuti zitiphunzitse ife. Malembowo amatilimbikitsa ndi kutithuzitsa mtima, kuti tizikhala ndi chiyembekezo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:26

Adachita zimenezi kuti aupatule ukhale wakewake, atauyeretsa pakuutsuka ndi madzi ndiponso ndi mau ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:18

Tsekulani maso anga kuti ndiwone zodabwitsa zochokera m'malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 6:18

Motero pali zinthu ziŵirizi, lonjezo ndi lumbiro, zimene sizingathe kusinthika, ndipo Mulungu sanganamirepo. Mwa zimenezi Mulungu adafuna kutilimbitsa mtima ife amene tidathaŵira kwa Iye, kuti tichigwiritse chiyembekezo chimene adatiikira pamaso pathu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 3:10

Mulungu adapitiriza nati, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetsetu zonse zimene ndikukuuza, ndipo uzikumbukire.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:24

Malamulo anu amandikondwetsa, ndiwo amene amandilangiza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:14

Kuyenda m'njira ya malamulo anu kumandikondwetsa, kupambana kukhala ndi chuma chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:148

Ndimakhala maso usiku wonse, ndikusinkhasinkha za malonjezo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 8:3

Adakutsitsani pokukhalitsani ndi njala, komanso adakupatsani mana kuti mudye. Inu ndi makolo anu simudadyepo ndi kale lonse chakudya chimenechi. Adachita zimenezi kuti akuphunzitseni kuti munthu sakhala ndi moyo ndi chakudya chokha ai, koma ndi mau onse otuluka m'kamwa mwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu wanga, wamkulu ndi wokhulupirika! Ndikukuyamikani chifukwa cha mawu anu, chifukwa kudzera mwa iwo ndimalandira chitsogozo chanu ndi chilango chanu. Mawu anu ndi amoyo, ndi amphamvu, akuthwa kuposa lupanga lakuthwa konsekonse, ndiwo anditsutsa, andiphunzitsa, ndi kundilangiza. Ndikupempha kuti mawu anu awululidwe mwa ine. Zikomo chifukwa ndi chakudya changa chabwino koposa ndipo mmenemo muli kukula kwanga kwauzimu. Ndiwo andisintha ndi kundipatsa moyo, akuulula zobisika zomwe zili mkati mwanga, akuzindikira zolinga za mtima wanga. Ambuye, mawu anu amati: "Wokhulupirira iwe, mitsinje ya madzi amoyo idzatuluka m'mimba mwake." Ndiwo amaunikira njira yanga ndi kunditeteza kuti ndisagwe. Ndipatseni nzeru zanu kuti ndikudziweni ndi kukumvetsani kudzera mwa iwo. M'dzina la Yesu. Ameni.