Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

63 Mau a Mulungu Okhudza Kuchita Chifuniro Chake

Monga mwana wa Mulungu, ndili ndi mwayi waukulu wotsogozedwa ndi Atate wanga wakumwamba, amene ali ndi nzeru zonse ndi mphamvu zonse. Iye amadziwa njira iliyonse yomwe ndikuyenda ndipo akufunitsitsa kundionetsa njira yabwino yoti nditsatire.

Mu Masalmo 321, pali lonjezo lamphamvu: "Ndidzakulangiza, ndidzakusonyeza njira yoyenera kupitamo; ndidzakupatsa uphungu, maso anga adzakhala pa iwe." Ndikafunafuna chifuniro cha Mulungu pa chisankho chilichonse, sindingasochere. Ndikungofunika kuzindikira ndi kudzilola kutsogozedwa ndi Mzimu Woyera pa chisankho chilichonse, chifukwa Iye amadziwa chomwe chili chabwino kwa ine.

Kudalira Yesu kumatanthauza kupambana pa chilichonse chimene ndichita. Kumbukira kuti chifuniro cha Mulungu kwa ine n’chabwino, chokondweretsa, ndiponso changwiro, ngakhale ndisanayambe kuchita zinthu m’njira yanga. Lolani Ambuye alembe nkhani yatsopano kwa ine, kumene chilichonse chidzagwirizana ndi chifuniro Chake, kumene maganizo anga sadzakhala patsogolo, koma zomwe Mulungu akufuna kwa ine.


1 Atesalonika 5:18

Muzithokoza Mulungu pa zonse. Paja zimene Mulungu amafuna kuti muzichita mwa Khristu Yesu nzimenezi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:17

Ndipotu dziko lapansi likupita, pamodzi ndi zake zonse zimene anthu amazilakalaka. Koma munthu wochita zimene Mulungu afuna, amakhalapo mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:1

Ndine, Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwa kufuna kwa Mulungu. Ndikulembera anthu a Mulungu amene ali ku Efeso, amenenso ali okhulupirika mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 143:10

Phunzitseni, kuti ndizichita zofuna Inu, pakuti ndinu Mulungu wanga. Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:36

Pafunikadi kupirira, kuti muchite zimene Mulungu akufuna, kuti motero mukalandire zimene adalonjeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:17

Nchifukwa chake musakhale opusa, koma dziŵani zimene Ambuye afuna kuti muchite.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:8

Ndimakonda kuchita zimene mumafuna, Inu Mulungu wanga, malamulo anu ali mumtima mwanga.”

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:10

Ufumu wanu udze. Kufuna kwanu kuchitidwe, monga kumwamba chomwechonso pansi pano.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 4:3

Chimene Mulungu akufuna ndi ichi: mukhale oyera mtima, ndiye kuti muzipewa dama.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 7:17

Aliyense wofuna kuchita kufuna kwa Mulungu, adzadziŵa ngati zimene Ine ndimalankhula nzochokera kwa Mulungu kapena kwa Ine ndekha.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:27

Ndipo Mulungu amene amayang'ana za m'kati mwa mitima ya anthu, amadziŵa zimene Mzimu Woyera afuna, pakuti Mzimuyo amapempherera anthu a Mulungu monga momwe Mulungu afunira.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 1:3-4

Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu akukomereni mtima ndi kukupatsani mtendere.

Khristuyo adadzipereka chifukwa cha machimo athu, kuti atipulumutse ku njira za moyo woipa uno. Pakutero adachita zimene Mulungu Atate athu ankafuna.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 22:42

Adati, “Atate, ngati mukufuna, mundichotsere chikho chamasautsochi. Komabe muchite zimene mukufuna Inu, osati zimene ndikufuna Ine ai.”

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:6

Musazichite mwachiphamaso chabe, ngati kuti mukungofuna kukondweretsa anthu. Koma ngati akapolo a Khristu, muzichita ndi mtima wonse zimene Mulungu afuna.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:17

Nkwabwino kumva zoŵaŵa chifukwa chochita zabwino, ngati Mulungu wafuna choncho, koposa kumva zoŵaŵa chifukwa chochita zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:19

Nchifukwa chake anthu amene amamva zoŵaŵa monga Mulungu afunira, adzipereke m'manja mwa Mlengi wao wokhulupirika, ndi kumachitabe ntchito zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 6:40

Pakuti chimene Atate anga afuna nchakuti munthu aliyense amene aona Mwanayo namkhulupirira, akhale ndi moyo wosatha; ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 6:39

Ndipo chofuna Iye amene adandituma nchakuti ndisatayepo ndi mmodzi yemwe mwa amene Iye adandipatsa, koma onse ndidzaŵaukitse kwa akufa pa tsiku lomaliza.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:15

Paja Mulungu amafuna kuti ndi zochita zanu zabwino muthetse kulankhula kosadziŵa kwa anthu opusa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:2

Musamatsanzira makhalidwe a anthu odalira zapansipano, koma Mulungu asinthe moyo wanu wonse pakukupatsani mitima yatsopano. Pamenepo mudzatha kudziŵa zimene Mulungu afuna, ndipo mudzazindikira zimene zili zabwino, zangwiro ndi zomkondwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 9:31

Timadziŵa kuti Mulungu samvera anthu ochimwa. Koma munthu akasamala za Mulungu, nachita zimene Mulungu afuna, Mulungu amamumvera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 1:12-13

Komabe ena adaamlandira nakhulupirira dzina lake, ndipo ameneŵa Iye adaŵapatsa mphamvu zoti akhale ana a Mulungu.

Kukhala ana a Mulungu kumeneku sikudachokere m'kubadwa kwao, kapena ku chifuniro cha thupi, kapena ku chifuniro cha munthu ai, koma kudachokera kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 18:14

Chonchonso Atate anu amene ali Kumwamba safuna kuti ndi mmodzi yemwe mwa anaŵa atayike.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:21

“Si munthu aliyense womangonditi ‘Ambuye, Ambuye’ amene adzaloŵe mu Ufumu wakumwamba ai. Koma adzaloŵe ndi wochita zimene Atate anga akumwamba afuna.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:16-17

Paja zonse zapansipano, zilakolako zathupi, zinthu zimene maso amakhumbira, ndiponso kunyadira za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku mkhalidwe woipa wa dziko lapansi.

Ndipotu dziko lapansi likupita, pamodzi ndi zake zonse zimene anthu amazilakalaka. Koma munthu wochita zimene Mulungu afuna, amakhalapo mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 3:35

Aliyense wochita zimene Mulungu akufuna, ameneyo ndiye mbale wanga ndi mlongo wanga ndi amai anga.”

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:20-21

Mulungu wopatsa mtendere, adaukitsa kwa akufa Ambuye athu Yesu, amene ndiye Mbusa wamkulu wa nkhosa, chifukwa cha imfa yake yotsimikizira Chipangano chamuyaya.

Mulunguyo akupatseni zabwino zonse zimene mukusoŵa kuti muzichita zimene Iye afuna. Ndipo mwa Yesu Khristu achite mwa ife zomkondweretsa, Khristuyo akhale ndi ulemerero mpaka muyaya. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:21

Tamandani Chauta, inu magulu a ankhondo ake onse, atumiki ake ochita zimene Iye afuna.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 12:50

Pakuti aliyense wochita zimene Atate anga akumwamba akufuna, ameneyo ndiye mbale wanga ndi mlongo wanga ndi amai anga.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 29:11

Zoona, Ine ndiye amene ndimadziŵa zimene ndidakukonzerani, zakuti mudzakhala pabwino osati poipa, kuti mukhale ndi chiyembekezo chenicheni pa zakutsogolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:46

“Bwanji mumangoti, ‘Ambuye, Ambuye,’ koma chonsecho simuchita zimene ndimanena?

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 6:38

Pajatu ndidatsika kuchokera Kumwamba kudzachita zofuna za Iye amene adandituma, osati kuti ndidzachite zofuna Ine ai.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:13

Paja Mulungu ndiye amene amagwira ntchito mwa inu, muzifuna ndi kutha kuchita zimene zimkomera Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 4:34

Koma Yesu adati, “Chakudya changa nkuchita zimene afuna Atate amene adandituma, kuti nditsirize ntchito imene Iwo adandipatsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 1:10

Kodi ponena zimenezi ndiye kuti ndikufuna kuti anthu andivomereze? Iyai, koma kuti andivomereze ndi Mulungu. Kodi ndikuyesa kukondweretsa anthu? Ndikadayesabe kukondweretsa anthu, si bwenzi ndilinso mtumiki wa Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 11:2

Yesu adati, “Pamene mukupemphera muziti, “ ‘Atate, dzina lanu lilemekezedwe. Ufumu wanu udze.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:39

Adapita patsogolo pang'ono, nadzigwetsa choŵeramitsa nkhope pansi nkuyamba kupemphera. Adati, “Atate, ngati nkotheka, chindichokere chikho chamasautsochi. Komabe chitani zimene mukufuna Inu, osati zimene ndikufuna Ine ai.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:15

Kwenikweni muyenera kumanena kuti, “Ambuye akalola, tikakhala ndi moyo, tidzachita chakutichakuti.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:105

mau anu ndiye nyale ya mapazi anga, ndipo amaunikira njira yanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 14:8

Tikakhala ndi moyo, moyowo ndi wa Ambuye, tikafa, timafera Ambuye. Nchifukwa chake, ngakhale tikhale ndi moyo kapena tife, ndife ao a Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:4-5

Mundidziŵitse njira zanu, Inu Chauta, mundiphunzitse kuchita kufuna kwanu.

Munditsogolere m'choona chanu ndi kundilangiza, pakuti Inu ndinu Mulungu Mpulumutsi wanga, ndimadalira Inu masiku onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 41:10

Usachite mantha chifukwa Ine ndili nawe, usataye mtima, poti Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu, ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:14

Inu ndinu abwenzi anga ngati muchita zimene ndikulamulani.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 1:4

Khristuyo adadzipereka chifukwa cha machimo athu, kuti atipulumutse ku njira za moyo woipa uno. Pakutero adachita zimene Mulungu Atate athu ankafuna.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:16-18

Khalani okondwa nthaŵi zonse.

Muzipemphera kosalekeza.

Muzithokoza Mulungu pa zonse. Paja zimene Mulungu amafuna kuti muzichita mwa Khristu Yesu nzimenezi.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:21

Mulunguyo akupatseni zabwino zonse zimene mukusoŵa kuti muzichita zimene Iye afuna. Ndipo mwa Yesu Khristu achite mwa ife zomkondweretsa, Khristuyo akhale ndi ulemerero mpaka muyaya. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:5-6

Uzikhulupirira Chauta ndi mtima wako wonse, usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.

Pa ntchito zako zonse uzivomera kuti kuli Mulungu, choncho njira zako Iye adzazilungamitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:10-11

Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse, musalole kuti ndisiye kumvera malamulo anu.

Ndili ndi nzeru kupambana okalamba, pakuti ndimatsata malamulo anu.

Ndimaletsa miyendo yanga kuti isayende m'njira yoipa iliyonse, kuti choncho ndizisunga mau anu.

Sindisiyana nawo malangizo anu, pakuti Inu mudandiphunzitsa

mau anu ndi otsekemera kwambiri ndikaŵalaŵa. Amatsekemera kuposa uchi m'kamwa mwanga.

Ndimakhala ndi nzeru za kumvetsa chifukwa cha malamulo anu. Nchifukwa chake ndimadana ndi njira iliyonse yonyenga.

mau anu ndiye nyale ya mapazi anga, ndipo amaunikira njira yanga.

Ndalumbirira, ndipo ndatsimikiza kuti ndidzamvera malangizo anu olungama.

Ndazunzika koopsa, Chauta, patseni moyo, molingana ndi mau anu aja.

Chauta, landirani mapemphero anga oyamika, ndipo mundiphunzitse malangizo anu.

Moyo wanga uli m'zoopsa nthaŵi zonse, komabe sindiiŵala malamulo anu.

Ndasunga mau anu mumtima mwanga, kuti ndisakuchimwireni.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:28

Ndipo tikudziŵa kuti Mulungu amayendetsa zinthu mwa njira yoti zonse ziŵakomere anthu omukonda ndipo apindulepo. Anthuwo ndi amene Iye amaŵaitana monga momwe Iye adazikonzera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:4

Kondwa mwa Chauta, ndipo adzakupatsa zimene mtima wako ukukhumba.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 10:31

Tsono, kaya mulikudya, kaya mulikumwa, kaya mukuchita chilichonse, muzichita zonse kuti mulemekeze Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 5:9

Nchifukwa chake, ngakhale tikhalebe kuno, kapena tikakhale kwa Ambuye, timayesetsa kuŵakondweretsa Ambuyewo.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:6

Sindikayika konse kuti Mulungu, amene adayamba kuchita ntchito yabwinoyi mwa inu, adzaipitiriza mpaka itatsirizika pa Tsiku la Kubweranso kwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:2

Ngodala amene amasunga malamulo a Chauta, amene amafunafuna Chauta ndi mtima wao wonse,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:14-15

Ndipo timalimba mtima pamaso pa Mulungu, popeza kuti amatimvera tikapempha kanthu kalikonse komukomera.

Ndipo ngati tikudziŵa kuti amatimvera tikapempha kanthu kalikonse, timadziŵanso kuti talandiradi zimene tampempha.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:3

Uike ntchito zako m'manja mwa Chauta, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:30

Tsono ndikukupemphani abale, kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu, ndiponso ndi chithandizo cha chikondi chimene Mzimu Woyera amapereka, kuti mugwirizane nane polimbikira kundipempherera kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:27

Mundidziŵitse mfundo za malamulo anu, ndipo ndidzasinkhasinkha za ntchito zanu zodabwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 2:10

Mulungu ndiye adatipanga. Adatilenga mwa Khristu Yesu kuti moyo wathu ukhale wogwira ntchito zabwino zimene Iye adakonzeratu kuti tizichite.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:13

Inu abale, Mulungu adakuitanani kuti mukhale mfulu. Koma chenjerani kuti ufulu wanu umenewu usapatse mpata khalidwe lanu lokonda zoipa. Kwenikweni muzitumikirana mwachikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:16

Chomwechonso inuyo muziwonetsa kuŵala kwanu pamaso pa anthu, kuti ataona ntchito zanu zabwino azilemekeza Atate anu akumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:23-24

Chilichonse chimene mungachite, muchichite ndi mtima wonse, ngati kuti mukuchitira Ambuye, osati anthu ai.

Paja mukudziŵa kuti Ambuye adzakupatsani mphotho. Mphothoyo ndi madalitso amene adalonjeza kudzapatsa anthu ake. Ambuye amene mukuŵatumikirawo ndi Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga, dzina lanu ndi loyera ndi loopsa, palibe chofanana ndi kuyera kwanu! Ndikubwera kwa inu kudzera mwa Ambuye wathu Yesu Khristu, ndikupemphani kuti mundithandize kukhala mogwirizana ndi chifuniro chanu ndikupha ine mwini, kudzikuza kwanga, ndikutha kusiya zokondweretsa zanga ndikumvetsa kuti chifuniro chanu ndi chabwino, chokondweretsa ndi changwiro pa moyo wanga. Mawu anu amati: "Chifukwa chake, musakhale opusa, koma dziwani chifuniro cha Ambuye." Atate, m'nthawi yovutayi mundithandize kuzindikira poganiza zochita ndipo osadzakhala wopusa patsogolo pa dziko lino, koma kukhala ndi nzeru yochokera kumwamba kuti nditsogoleredwe ndi Mzimu wanu Woyera, chifukwa chitsimikizo chokha cha chipambano changa ndi kukhala paubwenzi wolimba ndi inu. Ambuye, ndikupemphani kuti musunge mtima wanga ndi kundiphunzitsa tsiku lililonse kuchita zomwe mukufuna ndikupanga zisankho zoyenera, chifukwa zimenezo zidzasonyeza chifuniro chanu ndipo zidzabweretsa madalitso pa moyo wanga. Tsatani ulendo wanga wa tsiku ndi tsiku, kuti ndimvetse tsiku lililonse kuti sizokhudza ine koma inu. M'dzina la Yesu, Ameni.