Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

74 Mau a Mulungu Otonthoza Mtima

Ndikufuna ndikuuzeni kuti Malemba amatilonjeza kuti Mulungu ali ndi dongosolo la moyo wanu, dongosolo lodzaza ndi chiyembekezo ndi cholinga. Mukakumana ndi zovuta, kumbukirani mawu a pa Salmo 34:18 akuti, “Yehova ali pafupi ndi iwo a mtima wosweka, napulumutsa iwo a mzimu wolapa.” Khulupirirani kuti Mulungu adzakuthandizani ndi kukupatsani mphamvu kuti mudutse mumavuto onse.

Komanso, Yeremiya 29:11 amati, “Pakuti Ine ndidziwa malingaliro amene ndimaganizira inu, ati Yehova, malingaliro a mtendere, osati a choipa, kukupatsani inu chiyembekezo ndi tsogolo.” Mawu awa anditonthoza kwambiri ndipo amatikumbutsa kuti sitili tokha m’mavuto athu. Tiyeni tipitirize kukhala ndi chikhulupiriro mwa Ambuye, podziwa kuti chikondi chake ndi kukoma mtima kwake zili nafe nthawi zonse.


Masalimo 31:24

Limbikani ndipo Iye adzalimbitsa mtima wanu, inu nonse akuyembekeza Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:35-36

Potero musataye kulimbika kwanu, kumene kuli nacho chobwezera mphotho chachikulu.

Pakuti chikusowani chipiriro, kuti pamene mwachita chifuniro cha Mulungu, mukalandire lonjezano.

Mutu    |  Mabaibulo
Nahumu 1:7

Yehova ali wabwino, ndiye polimbikirapo tsiku la msauko; ndipo adziwa iwo omkhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 51:12

Ine, Inedi, ndine amene nditonthoza mtima wako; kodi iwe ndani, kuti uopa munthu amene adzafa, ndi mwana wa munthu amene adzakhala ngati udzu;

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 31:6

Khalani amphamvu, limbikani mitima, musamachita mantha, kapena kuopsedwa chifukwa cha iwowa; popeza Yehova Mulungu wanu ndiye amene amuka nanu; Iye sadzakusowani, kapena kukusiyani.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:1-2

Iye amene akhala pansi m'ngaka yake ya Wam'mwambamwamba adzagonera mu mthunzi wa Wamphamvuyonse.

palibe choipa chidzakugwera, ndipo cholanga sichidzayandikiza hema wako.

Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, akusunge m'njira zako zonse.

Adzakunyamula pa manja ao, ungagunde phazi lako pamwala.

Udzaponda mkango ndi mphiri; udzapondereza msona wa mkango ndi chinjoka.

Popeza andikondadi ndidzampulumutsa; ndidzamkweza m'mwamba, popeza adziwa dzina langa.

Adzandifuulira Ine ndipo ndidzamyankha; kunsautso ndidzakhala naye pamodzi; ndidzamlanditsa, ndi kumchitira ulemu.

Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri, ndi kumuonetsera chipulumutso changa.

Ndidzati kwa Yehova, Pothawirapo panga ndi linga langa; Mulungu wanga, amene ndimkhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:4

Inde, ndingakhale ndiyenda m'chigwa cha mthunzi wa imfa, sindidzaopa choipa; pakuti Inu muli ndi ine; chibonga chanu ndi ndodo yanu, izi zindisangalatsa ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 14:1

Mtima wanu usavutike; mukhulupirira Mulungu, khulupirirani Inenso.

Mutu    |  Mabaibulo
Nehemiya 8:10

Nanena naonso, Mukani, mukadye zonona, mukamwe zozuna, nimumtumizire gawo lake iye amene sanamkonzeretu kanthu; chifukwa lero ndilo lopatulikira Ambuye wathu; ndipo musamachita chisoni; pakuti chimwemwe cha Yehova ndicho mphamvu yanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Habakuku 3:17-18

Chinkana mkuyu suphuka, kungakhale kulibe zipatso kumpesa; yalephera ntchito ya azitona, ndi m'minda m'mosapatsa chakudya; ndi zoweta zachotsedwa kukhola, palibenso ng'ombe m'makola mwao;

koma ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasekerera mwa Mulungu wa chipulumutso changa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 12:2

Taonani, Mulungu ndiye chipulumutso changa; ndidzakhulupirira, sindidzaopa; pakuti Yehova Mwini ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, Iye ndiye chipulumutso changa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:28

Ndipo tidziwa kuti amene akonda Mulungu zinthu zonse zithandizana kuwachitira ubwino, ndiwo amene aitanidwa monga mwa kutsimikiza kwa mtima wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 143:8

Mundimvetse chifundo chanu mamawa; popeza ndikhulupirira Inu: Mundidziwitse njira ndiyendemo; popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 20:7-8

Ena atama magaleta, ndi ena akavalo; koma ife tidzatchula dzina la Yehova Mulungu wathu.

Iwowa anagonjeka, nagwa; koma ife tauka, ndipo takhala chilili.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:18

Yehova ali pafupi ndi iwo a mtima wosweka, apulumutsa iwo a mzimu wolapadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:1-2

Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.

Andigonetsa kubusa lamsipu, anditsogolera kumadzi odikha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 27:3

Lingakhale gulu la ankhondo limanga misasa kuti andithyole, mtima wanga sungachite mantha; ingakhale nkhondo ikandiukira, inde pomweponso ndidzakhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 18:2

Yehova ndiye thanthwe langa, ndi linga langa, ndi Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga, ngaka yanga, ndidzakhulupirira Iye; chikopa changa, nyanga ya chipulumutso changa, msanje wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:24-26

Ukagona, sudzachita mantha; udzagona tulo tokondweretsa.

Usaope zoopsa zodzidzimutsa, ngakhale zikadza zopasula oipa;

pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako, nadzasunga phazi lako lingakodwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 13:5-6

Koma ine ndakhulupirira pa chifundo chanu; mtima wanga udzakondwera nacho chipulumutso chanu.

Ndidzaimbira Yehova, pakuti anandichitira zokoma.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako;

umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:11-12

Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa; Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero; sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.

Yehova wa makamu, wodala munthu wakukhulupirira Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 42:5

Udziweramiranji moyo wanga iwe? Ndi kuzingwa m'kati mwanga? Yembekeza Mulungu, pakuti ndidzamyamikanso chifukwa cha chipulumutso cha nkhope yake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 4:8

Ndi mtendere ndidzagona pansi, pomwepo ndidzagona tulo; chifukwa Inu, Yehova, mundikhalitsa ine, ndikhale bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 22:31

Kunena za Mulungu, njira yake ili yangwiro; mau a Yehova anayesedwa; Iye ndiye chikopa kwa onse akukhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:4

Wodala munthuyo wakuyesa Yehova wokhulupirika; wosasamala odzikuza, ndi opatukira kubodza.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 11:18

Ndipo udzalimbika mtima popeza pali chiyembekezo; nudzafunafuna, ndi kugona mosatekeseka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:3-4

Khulupirira Yehova, ndipo chita chokoma; khala m'dziko, ndipo tsata choonadi.

Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru, ndi lilime lake linena chiweruzo.

Malamulo a Mulungu wake ali mumtima mwake; pakuyenda pake sadzaterereka.

Woipa aunguza wolungama, nafuna kumupha.

Yehova sadzamsiya m'dzanja lake; ndipo sadzamtsutsa poweruzidwa iye.

Yembekeza Yehova, nusunge njira yake, ndipo Iye adzakukweza kuti ulandire dziko. Pakudulidwa oipa udzapenya.

Ndapenya woipa, alikuopsa, natasa monga mtengo wauwisi wanzika.

Koma anapita ndipo taona, kwati zii; ndipo ndinampwaira osampeza.

Tapenya wangwiro, ndipo taona woongoka mtima! Pakuti ku matsiriziro ake a munthuyo kuli mtendere.

Koma olakwa adzaonongeka pamodzi; matsiriziro a oipa adzadulidwa.

Koma chipulumutso cha olungama chidzera kwa Yehova, Iye ndiye mphamvu yao m'nyengo ya nsautso.

Udzikondweretsenso mwa Yehova; ndipo Iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 16:1-2

Ndisungeni ine, Mulungu: pakuti ndakhulupirira Inu.

Pakuti simudzasiya moyo wanga kumanda; simudzalola wokondedwa wanu avunde.

Mudzandidziwitsa njira ya moyo, pankhope panu pali chimwemwe chokwanira; m'dzanja lanu lamanja muli zokondweretsa zomka muyaya.

Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Ambuye wanga, ndilibe chabwino china choposa Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 46:1

Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu m'masautso.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:3

M'mawa, Yehova, mudzamva mau anga; m'mawa, ndidzakukonzerani pemphero langa, ndipo ndidzadikira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:50

Chitonthozo changa m'kuzunzika kwanga ndi ichi; pakuti mau anu anandipatsa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 30:5

Mau onse a Mulungu ali oyengeka; ndiye chikopa cha iwo amene amkhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 7:10

Chikopa changa chili ndi Mulungu, wopulumutsa oongoka mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:11-12

Koma akondwere onse amene athawira kwa Inu, afuule mokondwera kosaleka, popeza muwafungatira; nasekere mwa Inu iwo akukonda dzina lanu.

Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungamayo; mudzamtchinjiriza nacho chivomerezo ngati chikopa.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 3:4-6

Ndipo kulimbika kotere kwa Mulungu tili nako mwa Khristu:

si kuti tili okwanira pa ife tokha, kuyesera kanthu monga mochokera mwa ife tokha; kukwanira kwathu kuchokera kwa Mulungu;

amenenso anatikwaniritsa ife tikhale atumiki a pangano latsopano; si la chilembo, koma la mzimu; pakuti chilembo chipha, koma mzimu uchititsa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 22:4-5

Makolo athu anakhulupirira Inu; anakhulupirira, ndipo munawalanditsa.

Anafuula kwa Inu, napulumutsidwa; anakhulupirira Inu, ndipo sanachite manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:3

Achiritsa osweka mtima, namanga mabala ao.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 41:10

usaope, pakuti Ine ndili pamodzi ndi iwe; usaopsedwe, pakuti Ine ndine Mulungu wako; ndidzakulimbitsa; inde, ndidzakuthangata; inde, ndidzakuchirikiza ndi dzanja langa lamanja la chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 61:1

Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine; pakuti Yehova wandidzoza ine ndilalikire mau abwino kwa ofatsa; Iye wanditumiza ndikamange osweka mtima, ndikalalikire kwa am'nsinga mamasulidwe, ndi kwa omangidwa kutsegulidwa kwa m'ndende;

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:4

Odala ali achisoni; chifukwa adzasangalatsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 14:16-17

Ndipo Ine ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani inu Nkhoswe ina, kuti akhale ndi inu kunthawi yonse,

ndiye Mzimu wa choonadi; amene dziko lapansi silingathe kumlandira, pakuti silimuona Iye, kapena kumzindikira Iye. Inu mumzindikira Iye; chifukwa akhala ndi inu nadzakhala mwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 1:3-4

Wolemekezeka Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Atate wa zifundo ndi Mulungu wa chitonthozo chonse,

wotitonthoza ife m'nsautso yathu yonse, kuti tidzathe ife kutonthoza iwo okhala m'nsautso iliyonse, mwa chitonthozo chimene titonthozedwa nacho tokha ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:6-7

Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi chiyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu.

Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana chidziwitso chonse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 5:7

ndi kutaya pa Iye nkhawa yanu yonse, pakuti Iye asamalira inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:13

Ndipo Mulungu wa chiyembekezo adzaze inu ndi chimwemwe chonse ndi mtendere m'kukhulupirira, kuti mukachuluke ndi chiyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Maliro 3:31-33

Pakuti Ambuye sadzataya kufikira nthawi zonse.

Angakhale aliritsa, koma adzachitira chisoni monga mwa kuchuluka kwa zifundo zake.

Pakuti samasautsa dala, ngakhale kumvetsa ana a anthu chisoni.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:15-16

Pakuti sitili naye mkulu wa ansembe wosatha kumva chifundo ndi zofooka zathu; koma wayesedwa m'zonse monga momwe ife, koma wopanda uchimo.

Potero tilimbike mtima poyandikira mpando wachifumu wachisomo, kuti tilandire chifundo ndi kupeza chisomo cha kutithandiza nthawi yakusowa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 30:5

Pakuti mkwiyo wake ukhala kanthawi kokha; koma kuyanja kwake moyo wonse. Kulira kuchezera, koma mamawa kuli kufuula kokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 73:26

Likatha thupi langa ndi mtima wanga, Mulungu ndiye thanthwe la mtima wanga, ndi cholandira changa chosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 94:19

Pondichulukira zolingalira zanga m'kati mwanga, zotonthoza zanu zikondweretsa moyo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 12:1

Tsiku lomwelo udzati, Ndikuyamikani inu Yehova; pakuti ngakhale munandikwiyira, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mutonthoza mtima wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:1

Mutonthoze, mutonthoze mtima wa anthu anga, ati Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:18

Pakuti ndiyesa kuti masauko a nyengo yatsopano sayenera kulinganizidwa ndi ulemerero umene udzaonetsedwa kwa ife.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 4:17

Pakuti chisautso chathu chopepuka cha kanthawi chitichitira ife kulemera koposa kwakukulu ndi kosatha kwa ulemerero;

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:6

pokhulupirira pamenepo, kuti Iye amene anayamba mwa inu ntchito yabwino, adzaitsiriza kufikira tsiku la Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 126:5

Akubzala ndi misozi adzatuta ndi kufuula mokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:76

Chifundo chanu chikhaletu chakunditonthoza, ndikupemphani, monga mwa mau anu kwa mtumiki wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:28

Moyo wanga wasungunuka ndi chisoni: Mundilimbitse monga mwa mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 11:28-30

Idzani kuno kwa Ine nonsenu akulema ndi kuthodwa, ndipo Ine ndidzakupumulitsani inu.

Senzani goli langa, ndipo phunzirani kwa Ine; chifukwa ndili wofatsa ndi wodzichepetsa mtima: ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu.

nati kwa Iye, Inu ndinu wakudza kodi, kapena tiyembekezere wina?

Pakuti goli langa lili lofewa, ndi katundu wanga ali wopepuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:1-3

Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.

Andigonetsa kubusa lamsipu, anditsogolera kumadzi odikha.

Atsitsimutsa moyo wanga; anditsogolera m'mabande a chilungamo, chifukwa cha dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 49:13

Imbani inu, m'mwamba, nukondwere iwe dziko lapansi, imbani inu mapiri, pakuti Yehova watonthoza mtima wa anthu ake, nadzachitira chifundo ovutidwa ake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:11

Mwa ichi chenjezanani, ndipo mangiriranani wina ndi mnzake, monganso mumachita.

Mutu    |  Mabaibulo
Maliro 3:22-24

Chifukwa chakusathedwa ife ndicho chifundo cha Yehova, pakuti chisoni chake sichileka,

chioneka chatsopano m'mawa ndi m'mawa; mukhulupirika ndithu.

Moyo wanga uti, Gawo langa ndiye Yehova; chifukwa chake ndidzakhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:1-2

Ndimkonda, popeza Yehova amamva mau anga ndi kupemba kwanga.

Ndinakhulupirira, chifukwa chake ndinalankhula; ndinazunzika kwambiri.

Pofulumizidwa mtima ndinati ine, anthu onse nga mabodza.

Ndidzabwezera Yehova chiyani chifukwa cha zokoma zake zonse anandichitira?

Ndidzanyamula chikho cha chipulumutso, ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.

Ndidzachita zowinda zanga za kwa Yehova, tsopano, pamaso pa anthu ake onse.

Imfa ya okondedwa ake nja mtengo wake pamaso pa Yehova.

Ndiloleni, Yehova, indetu ndine mtumiki wanu; ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; mwandimasulira zondimanga.

Ndidzapereka kwa Inu nsembe yachiyamiko, ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.

Ndidzachita zowinda zanga za kwa Yehova, tsopano, pamaso pa anthu ake onse.

M'mabwalo a nyumba ya Yehova, pakati pa inu, Yerusalemu. Aleluya.

Popeza amanditcherera khutu lake, chifukwa chake ndidzaitanira Iye masiku anga onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:82

Maso anga anatha mphamvu ndi kukhumba mau anu, ndikuti, Mudzanditonthoza liti?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 107:13-14

Pamenepo anafuulira kwa Yehova mumsauko mwao, ndipo anawapulumutsa m'kupsinjika kwao.

Anawatulutsa mumdima ndi mu mthunzi wa imfa, nadula zomangira zao.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 1:7

Pakuti Mulungu sanatipatse mzimu wa mantha; komatu wa mphamvu ndi chikondi ndi chidziletso.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:18

Mulibe mantha m'chikondi; koma chikondi changwiro chitaya kunja mantha, popeza mantha ali nacho chilango, ndipo wamanthayo sakhala wangwiro m'chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 56:3

Tsiku lakuopa ine, ndidzakhulupirira Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 12:5

Chifukwa cha kupasuka kwa ozunzika, chifukwa cha kuusa moyo kwa aumphawi, ndiuka tsopano, ati Yehova; ndidzamlonga mosungika muja alakalakamo.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga Wamkulu ndi Wamphamvu, lero ndabwera pamaso panu, kudzera mwa Ambuye wanga Yesu Khristu, kukuthokozani. Pakati pa mavuto, inu mwakhala thandizo langa ndi mphamvu yanga. Pakati pa kusowa, mwandipezera zonse zofunikira. Ndipo nthawi zovuta pamene ambiri anandisiya, inu nokha munakhalabe nane. Zikomo chifukwa pakati pa mantha, Mzimu wanu Woyera wandipatsa kulimba mtima kukumana ndi mavuto ndi zovuta, ndipo ndapeza chigonjetso. Ambuye, pakati pa mtendere ndi chikhulupiriro, ndadziwa kuti ndinu Mulungu amene amanditsogolera munkondo zanga. Chifukwa chodikira moleza mtima, ndili ndi chiyembekezo cholandira zabwino koposa. M'dzina lamphamvu la Yesu. Ameni.