Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 13 - Buku Lopatulika


Munkhawa athawira Mulungu namkhulupirira
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Mudzandiiwala chiiwalire, Yehova, kufikira liti? Mudzandibisira ine nkhope yanu kufikira liti?

2 Ndidzachita uphungu m'moyo mwanga kufikira liti, pokhala ndi chisoni m'mtima mwanga tsiku lonse? Adzandiukira ine mdani wanga kufikira liti?

3 Penyani, ndiyankheni, Yehova Mulungu wanga. Penyetsani maso anga, kuti ndingagone tulo ta imfa;

4 kuti anganene mdani wanga, Ndamgonjetsa; ndipo angakondwere otsutsana nane posunthika ine.

5 Koma ine ndakhulupirira pa chifundo chanu; mtima wanga udzakondwera nacho chipulumutso chanu.

6 Ndidzaimbira Yehova, pakuti anandichitira zokoma.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa