Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 12 - Buku Lopatulika


Anthu ndi amabodza, Mulungu ndiye woona
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Seminiti. Salimo la Davide.

1 Pulumutsani, Yehova; pakuti wofatsa wasowa; pakuti okhulupirika achepa mwa ana a anthu.

2 Amanena za bodza munthu yense ndi mnansi wake, amanena ndi mlomo wothyasika, ndi mitima iwiri.

3 Yehova adzadula milomo yonse yothyasika, lilime lakudzitamandira;

4 amene amati, Ndi lilime lathu tidzaposa; milomo yathu nja ife eni; mbuye wa pa ife ndani?

5 Chifukwa cha kupasuka kwa ozunzika, chifukwa cha kuusa moyo kwa aumphawi, ndiuka tsopano, ati Yehova; ndidzamlonga mosungika muja alakalakamo.

6 Mau a Yehova ndi mau oona; ngati siliva woyenga m'ng'anjo yadothi, yoiyeretsa kasanu ndi kawiri.

7 Mudzawasunga, Yehova, mudzawatchinjirizira mbadwo uno kunthawi zonse.

8 Oipa amayenda mozungulirazungulira, potamanda iwo chonyansa mwa ana a anthu.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa