Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

65 Mau a Mulungu Okhudza Mphatso Yaulosi


1 Akorinto 12:10

ndi kwa wina machitidwe a mphamvu; ndi kwa wina chinenero; ndi kwa wina chizindikiro cha mizimu; kwa wina malilime a mitundumitundu; ndi kwa wina mamasulidwe a malilime.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 14:1

Tsatani chikondi; koma funitsitsani mphatso zauzimu, koma koposa kuti mukanenere.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 14:3

Koma iye wakunenera alankhula ndi anthu chomangirira ndi cholimbikitsa, ndi chosangalatsa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 14:4

Iye wakulankhula lilime, adzimangirira yekha, koma iye wakunenera amangirira Mpingo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 14:5

Ndipo ndifuna inu nonse mulankhule malilime, koma makamaka kuti mukanenere; ndipo wakunenera aposa wakulankhula malilime, akapanda kumasulira, kuti Mpingo ukalandire chomangirira.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 14:22

Chotero malilime akhala ngati chizindikiro, si kwa iwo akukhulupirira, koma kwa iwo osakhulupirira; koma kunenera sikuli kwa iwo osakhulupirira, koma kwa iwo amene akhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 14:24-25

Koma ngati onse anenera, ndipo alowamo wina wosakhulupirira kapena wosaphunzira, atsutsidwa ndi onse; aweruzidwa ndi onse;

zobisika za mtima wake zionetsedwa; ndipo chotero adzagwa nkhope yake pansi, nadzagwadira Mulungu, nadzalalikira kuti Mulungu ali ndithu mwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 14:29

Ndipo aneneri alankhule awiri kapena atatu, ndi ena azindikire.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 14:31

Pakuti mukhoza nonse kunenera mmodzimmodzi, kuti onse aphunzire, ndi onse afulumidwe;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 14:32

ndipo mizimu ya aneneri imvera aneneri;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 14:39

Chifukwa chake, abale anga, funitsitsani kunenera, ndipo musaletse kulankhula malilime.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:11

Ndipo Iye anapatsa ena akhale atumwi; ndi ena aneneri; ndi ena alaliki; ndi ena abusa, ndi ena aphunzitsi;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:6

Ndipo pokhala ife ndi mphatso zosiyana, monga mwa chisomo chipatsidwa kwa ife, kapena mphatso yakunenera, tinenere monga mwa muyeso wa chikhulupiriro;

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 2:17

Ndipo kudzali m'masiku otsiriza, anena Mulungu, ndidzathira cha Mzimu wanga pa thupi lililonse, ndipo ana anu aamuna, ndi aakazi adzanenera, ndipo anyamata anu adzaona masomphenya, ndi akulu anu adzalota maloto;

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 2:18

ndiponso pa akapolo anga ndi pa adzakazi anga m'masiku awa ndidzathira cha Mzimu wanga; ndipo adzanenera.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 11:27-28

Koma masiku awa aneneri anatsika ku Yerusalemu kudza ku Antiokeya.

Ndipo ananyamuka mmodzi wa iwo, dzina lake Agabu, nalosa mwa Mzimu, kuti padzakhala njala yaikulu padziko lonse lokhalamo anthu; ndiyo idadza masiku a Klaudio.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 13:1

Ndipo kunali aneneri ndi aphunzitsi ku Antiokeya mu Mpingo wa komweko, ndiwo Barnabasi, ndi Simeoni, wonenedwa Wakuda, ndi Lusio wa ku Kirene, Manaene woleredwa pamodzi ndi Herode chiwangacho, ndi Saulo.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 19:6

Ndipo pamene Paulo anaika manja ake pa iwo, Mzimu Woyera anadza pa iwo; ndipo analankhula ndi malilime, nanenera.

Mutu    |  Mabaibulo
Amosi 3:7

Pakuti Ambuye Yehova sadzachita kanthu osawulula chinsinsi chake kwa atumiki ake aneneri.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 1:9

Ndipo Yehova anatulutsa dzanja lake, nakhudza pakamwa panga; nati Yehova kwa ine, Taona ndaika mau anga m'kamwa mwako;

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 23:28

Mneneri wokhala ndi loto, anene loto lake; ndi iye amene ali ndi mau anga, anene mau anga mokhulupirika. Kodi phesi ndi chiyani polinganiza ndi tirigu? Ati Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 2:7

Ndipo ukanene nao mau anga, ngakhale akamva kapena akaleka kumva; pakuti iwo ndiwo opanduka.

Mutu    |  Mabaibulo
Yoweli 2:28

Ndipo kudzachitika m'tsogolo mwake, ndidzatsanulira mzimu wanga pa anthu onse, ndi ana aamuna ndi aakazi adzanenera, akuluakulu anu adzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya;

Mutu    |  Mabaibulo
Mika 3:8

Koma ine ndidzala nayo mphamvu mwa Mzimu ya Yehova, ndi chiweruzo, ndi chamuna, kufotokozera Yakobo kulakwa kwake, ndi kwa Israele tchimo lake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:20

Musanyoze manenero;

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 1:21

pakuti kale lonse chinenero sichinadze ndi chifuniro cha munthu; koma anthu a Mulungu, ogwidwa ndi Mzimu Woyera, analankhula.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 1:3

Wodala iye amene awerenga, ndi iwo amene akumva mau a chinenerocho, nasunga zolembedwa momwemo; pakuti nthawi yayandikira.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 19:10

Ndipo ndinagwa pa mapazi ake kumlambira iye. Ndipo ananena ndi ine, Tapenya, usatero; ine ndine kapolo mnzako, ndi mnzao wa abale ako akukhala nao umboni wa Yesu; lambira Mulungu: pakuti umboni wa Yesu ndiwo Mzimu wa chinenero.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 28:9

Mneneri amene anenera za mtendere, pamene mau a mneneri adzachitidwa, pamenepo mneneri adzadziwika, kuti Yehova anamtuma ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo
Numeri 12:6

Ndipo anati, Tamvani, tsono mau anga; pakakhala mneneri pakati pa inu, Ine Yehova ndidzizindikiritsa kwa iye m'masomphenya, ndinena naye m'kulota.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mafumu 20:1

Masiku ajawo Hezekiya anadwala, nafuna kufa. Namdzera Yesaya mneneri mwana wa Amozi, nanena naye, Atero Yehova, Siyira banja lako; pakuti udzafa, sudzakhala ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 3:20

Ndipo Aisraele onse, kuyambira ku Dani kufikira ku Beereseba anazindikira kuti Samuele anakhazikika akhale mneneri wa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 6:8

Ndipo ndinamva mau a Ambuye akuti, Ndidzatumiza yani, ndipo ndani adzatimukira ife? Ndipo ine ndinati, Ndine pano; munditumize ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 23:16

Yehova wa makamu atero, Musamvere mau a aneneri amene anenera kwa inu; akuphunzitsani zachabe; anena masomphenya a mtima wao, si a m'kamwa mwa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 30:10

amene amati kwa alauli, Mtima wanu usapenye; ndi kwa aneneri, Musanenere kwa ife zinthu zoona, munene kwa ife zinthu zamyadi, munenere zonyenga;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 22:14

Koma Mikaya anati, Pali Yehova, zimene Yehova adzanena nane ndidzanena ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 1:6

Koma mau anga ndi malemba anga, amene ndinalamulira atumiki anga aneneriwo, kodi sanawapeze makolo anu? Ndipo anabwera, nati, Monga umo Yehova wa makamu analingirira kutichitira ife, monga mwa njira zathu ndi monga mwa machitidwe athu, momwemo anatichitira.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:15

Yang'anirani mupewe aneneri onyenga, amene adza kwa inu ndi zovala zankhosa, koma m'kati mwao ali mimbulu yolusa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 24:24

chifukwa Akhristu onama adzauka, ndi aneneri onama nadzaonetsa zizindikiro zazikulu ndi zozizwa: kotero kuti akanyenge, ngati nkotheka, osankhidwa omwe. Onani ndakuuziranitu pasadafike.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 1:70

Monga Iye analankhula ndi m'kamwa mwa aneneri ake oyera mtima, akale lomwe,

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 3:18

Koma zimene Mulungu analalikiratu m'kamwa mwa aneneri onse, kuti adzamva kuwawa Khristu, Iye anakwaniritsa chotero.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mafumu 17:13

Ndipo Yehova anachitira umboni Israele ndi Yuda mwa dzanja la mneneri aliyense, ndi mlauli aliyense, ndi kuti, Bwererani kuleka ntchito zanu zoipa, nimusunge malamulo anga ndi malemba anga, monga mwa chilamulo chonse ndinachilamulira makolo anu, ndi kuchitumizira inu mwa dzanja la atumiki anga aneneri.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 14:14

Ndipo Yehova anati kwa ine, Aneneri anenera zonama m'dzina langa; sindinatume iwo, sindinauze iwo, sindinanene nao; anenera kwa inu masomphenya onama, ndi ula, ndi chinthu chachabe, ndi chinyengo cha mtima wao.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 13:3

Atero Ambuye Yehova, Tsoka aneneri opusawo akutsata mzimu waowao, chinkana sanaone kanthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 23:21

Sindinatuma aneneri awa, koma anathamanga; sindinanene ndi iwo, koma ananenera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 23:29

Kodi mau anga safanafana ndi moto? Ati Yehova, ndi kufanafana ndi nyundo imene iphwanya mwala?

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:41

Iye wakulandira mneneri, pa dzina la mneneri, adzalandira mphotho ya mneneri; ndipo wakulandira munthu wolungama, pa dzina la munthu wolungama adzalandira mphotho ya munthu wolungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 22:18

Ndichita umboni kwa munthu aliyense wakumva mau a chinenero cha buku ili, Munthu akaonjeza pa awa, adzamuonjezera Mulungu miliri yolembedwa m'bukumu:

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 10:11

Ndipo ananena nane, Uyenera iwe kuneneranso pa anthu ndi mitundu, ndi manenedwe, ndi mafumu ambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 18:22

Ndipo Eliya ananena ndi anthuwo, Ine ndatsala ndekha mneneri wa Yehova, koma aneneri a Baala ndiwo anthu mazana anai mphambu makumi asanu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mafumu 2:15

Ndipo pamene anampenya ana a aneneri okhala ku Yeriko pandunji pake, anati, Mzimu wa Eliya watera pa Elisa. Ndipo anadza kukomana naye, nadziweramitsa pansi kumaso kwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 13:2

Ndipo pa kutumikira Ambuye iwowa, ndi kusala chakudya, Mzimu Woyera anati, Mundipatulire Ine Barnabasi ndi Saulo ku ntchito imene ndinawaitanirako.

Mutu    |  Mabaibulo
Amosi 7:15

ndipo Yehova ananditenga ndilikutsata nkhosa, nati kwa ine Yehova, Muka, nenera kwa anthu anga Israele.

Mutu    |  Mabaibulo
Yona 3:4

Ndipo Yona anayamba kulowa mzindawo ulendo wa tsiku limodzi, nalalikira, nati, Atsala masiku makumi anai ndipo Ninive adzapasuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 37:4

Pamenepo anati kwa ine, Nenera kwa mafupa awa, nuti nao, Mafupa ouma inu, imvani mau a Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 12:7

Koma kwa yense kwapatsidwa maonekedwe a Mzimu kuti apindule nao.

Mutu    |  Mabaibulo
Danieli 9:24

Masabata makumi asanu ndi awiri alamulidwira anthu a mtundu wako ndi mzinda wako wopatulika, kumaliza cholakwacho, ndi kutsiriza machimo, ndi kutetezera mphulupulu, ndi kufikitsa chilungamo chosalekeza, ndi kukhomera chizindikiro masomphenya ndi zonenera, ndi kudzoza malo opatulika kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Zefaniya 3:17

Yehova Mulungu wako ali pakati pako, wamphamvu wakupulumutsa; adzakondwera nawe ndi chimwemwe, adzakhala wopanda thamo m'chikondi chake; adzasekerera nawe ndi kuimbirapo.

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 8:9

Atero Yehova wa makamu: Alimbike manja anu, inu akumva masiku ano mau awa pakamwa pa aneneri amene anakhalako tsiku lakuikidwa maziko a nyumba ya Yehova wa makamu, ndiyo Kachisi, kuti amangidwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Hoseya 12:10

Ndalankhulanso ndi aneneri, ndipo Ine ndachulukitsa masomphenya; ndi padzanja la aneneri ndinanena ndi mafanizo.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 13:9

Ndi dzanja langa lidzakhala lotsutsana nao aneneri akuona zopanda pake, ndi kupenda za bodza; sadzakhala mu msonkhano wa anthu anga, kapena kulembedwa m'buku lolembedwamo nyumba ya Israele; kapena kulowa m'dziko la Israele; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mbiri 20:20

Nalawira mamawa, natuluka kunka kuchipululu cha Tekowa; ndipo potuluka iwo, Yehosafati anakhala chilili, nati, Mundimvere ine, Ayuda inu, ndi inu okhala mu Yerusalemu, limbikani mwa Yehova Mulungu wanu, ndipo mudzakhazikika; khulupirirani aneneri ake, ndipo mudzalemerera.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 10:5-6

Ndipo m'tsogolo mwake mudzafika kuphiri la Mulungu, kumene kuli kaboma ka Afilisti; ndipo kudzali kuti pakufika inu kumzindako mudzakomana ndi gulu la aneneri, alikutsika kumsanje ndi chisakasa, ndi lingaka, ndi chitoliro, ndi zeze, pamaso pao; iwo adzanenera;

ndipo Mzimu wa Yehova udzagwera inu kolimba, nanunso mudzanenera pamodzi nao, nimudzasandulika munthu wina.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 19:16

ukadzozenso Yehu mwana wa Nimisi akhale mfumu ya Israele; ukadzozenso Elisa mwana wa Safati wa ku Abele-Mehola akhale mneneri m'malo mwako.

Mutu    |  Mabaibulo