Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Yona 3 - Buku Lopatulika


Yona ku Ninive. Kulapa kwa a ku Ninive

1 Ndipo mau a Yehova anadza kwa Yona nthawi yachiwiri, ndi kuti,

2 Nyamuka, pita ku Ninive mzinda waukulu uja, nuulalikire uthenga umene ndikuuza.

3 Ndipo Yona ananyamuka, napita ku Ninive, monga mwa mau a Yehova. Koma Ninive ndiwo mzinda waukulu pamaso pa Yehova, wa ulendo wa masiku atatu.

4 Ndipo Yona anayamba kulowa mzindawo ulendo wa tsiku limodzi, nalalikira, nati, Atsala masiku makumi anai ndipo Ninive adzapasuka.

5 Ndipo anthu a Ninive anakhulupirira Mulungu, nalalikira chosala, navala chiguduli, kuyambira wamkulu kufikira wamng'ono wa iwowa.

6 Pakuti mau awa anafikira mfumu ya Ninive, ndipo inanyamuka kumpando wake wachifumu, nivula chofunda chake, nifunda chiguduli, nikhala m'maphulusa.

7 Ndipo analalikira, nanena mu Ninive mwa lamulo la mfumu ndi nduna zake, ndi kuti, Ngakhale munthu kapena nyama, ngakhale ng'ombe kapena nkhosa, zisalawe kanthu, zisadye, zisamwe madzi;

8 koma zifundidwe ndi chiguduli munthu ndi nyama, ndipo zifuulire kolimba kwa Mulungu; ndipo abwere yense kuleka njira yake yoipa, ndi chiwawa chili m'manja mwake.

9 Kaya, akatembenuka Mulungu, ndi kuleka kubwera ku mkwiyo wake waukali, kuti tisatayike.

10 Ndipo Mulungu anaona ntchito zao, kuti anabwera kuleka njira yao yoipa; ndipo Mulungu analeka choipa adanenachi kuti adzawachitira, osachichita.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa