Ndikufuna ndikuuzani nkhani ya atumwi a Yesu. Iwo anakonzedwa mosamala kwambiri ndi Yesu kuti agwire ntchito yaikulu, chifukwa adzaona zinthu zazikulu kwambiri pa moyo wake, ndipo adzachitira umboni za kuuka kwake. Atumwi 12 amenewa anali mabwenzi ake omwe anali kuwadalira kwambiri. Ambiri anali ochokera ku Galileya, monga mmene Yesu analinso, ndipo ena anali okwatira.
Mawu a Mulungu mu Machitidwe 1:21-22 amati: "Chifukwa chake m'pofunika kuti mmodzi wa amuna amene anakhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu analowa ndi kutuluka pakati pathu, kuyambira ubatizo wa Yohane kufikira tsiku limene anakwezedwa kuchokera kwa ife, akhale mboni ya kuuka kwake pamodzi ndi ife." Apa, Petro akutiwonetsa kuti amene anali oyenerera kukhala atumwi ndi amene anakhalapo kuyambira ubatizo wa Yohane. Kenako, akutiuza kuti ayenera kukhala mboni za imfa ndi kuuka kwa Yesu. Chofunika kwambiri kwa munthu wofuna kukhala mtumwi chinali chakuti anakhalapo ndipo anaona Yesu mpaka tsiku limene anakwera kumwamba.
Mulungu adandiika kuti ndikhale mlaliki, mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwino umenewu,
Anthuwo ankasonkhana modzipereka kuti amve zimene atumwi ankaphunzitsa. Ankayanjana, ndipo ankadya Mgonero wa Ambuye ndi kupemphera pamodzi.
Iyeyu ndiye amene “adapereka mphatso kwa anthu.” Mphatso zake zinali zakuti ena akhale atumwi, ena aneneri, ena alaliki, ena abusa ndi aphunzitsi.
Ndinu omangidwa pamodzi m'nyumba yomangidwa pa maziko amene ndi atumwi ndi aneneri, ndipo Khristu Yesu mwini ndiye mwala wapangodya.
Yesu adasonkhanitsa ophunzira ake khumi ndi aŵiri aja, naŵapatsa mphamvu pa mizimu yoipitsa anthu, kuti aziitulutsa mwa anthuwo, ndiponso mphamvu zochiritsira nthenda zonse za anthu ndi zofooka zao zam'thupi.
Atumwi ankachita umboni ndi mphamvu yaikulu kuti Ambuye Yesu adaukadi kwa akufa, ndipo onse Mulungu ankaŵakomera mtima kwambiri.
Ndine, Paulo, mtumwi. Adandisankha si anthu ai, koma Yesu Khristu, ndiponso Mulungu Atate amene adamuukitsa kwa akufa.
Ndine, Paulo, mtumiki wa Yesu Khristu. Mulungu adandiitana kuti ndikhale mtumwi, nandipatula kuti ndikalalike Uthenga wake Wabwino.
Ndikuwona kuti atumwife Mulungu adatipatsa malo a kuthungo kwenikweni, ngati anthu oti akukaphedwa. Ndithu tasanduka ngati chinthu chochiwonetsa kwa zolengedwa zonse, osati anthu okha ai, komanso ndi angelo omwe.
Ndidakutsimikizirani mopirira kwambiri kuti ndine mtumwi, pakuchita pakati panu zizindikiro, zozizwitsa ndi ntchito zina zamphamvu.
Atumwi khumi ndi aŵiriwo maina ao ndi aŵa: Woyamba ndi Simoni, wotchedwa Petro, ndipo mbale wake Andrea; Yakobe, mwana wa Zebedeo, ndi mbale wake Yohane;
Pajatu odzalankhula si ndinu ai, koma Mzimu wa Atate anu ndiye amene adzalankhula kudzera mwa inu.
“Mbale azidzapereka mbale wake kuti aphedwe, bambo azidzapereka mwana wake. Ana adzaukira makolo ao, mpaka kuŵaphetsa.
Anthu onse adzadana nanu chifukwa cha Ine. Koma yemwe adzalimbikire mpaka potsiriza, ameneyo ndiye adzapulumuke.
Tsono akamadzakuzunzani ku mudzi wakutiwakuti, mukathaŵire ku mudzi wina. Ndithu ndikunenetsa kuti musanathe kuyendera midzi yonse ya Aisraele, Mwana wa Munthu adzakhala atabwera.
Paja wophunzira saposa mphunzitsi wake, ndipo wantchito saposa mbuye wake ai.
Kumkwanira wophunzira kuti alingane ndi mphunzitsi wake, ndiponso wantchito kuti alingane ndi mbuye wake. Tsono ngati mwini banja anthu adamutcha Belezebulu, nanji a m'banja mwake, kodi sadzaŵatcha maina oipa koposa apa?
“Choncho inu musamaopa anthu. Kanthu kalikonse kovundikirika kadzaululuka, ndipo kalikonse kobisika kadzadziŵika.
Zimene ndikukuuzirani m'chibisibisi, inu mukazilankhulire poyera, ndipo zimene mukuzimvera m'manong'onong'o, inu mukazilalikire pa madenga.
Musamaŵaopa amene amapha thupi, koma mzimu sangathe kuupha. Makamaka muziwopa amene angathe kuwononga thupi ndi mzimu womwe m'Gehena.
Suja amagulitsa atimba aŵiri kandalama kamodzi? Komabe palibe ndi m'modzi yemwe amene angagwe pansi, Atate anu osadziŵa.
Filipo ndi Bartolomeo; Tomasi ndi Mateyo, wokhometsa msonkho uja; Yakobe, mwana wa Alifeyo, ndi Tadeyo;
Inuyotu ngakhale tsitsi lomwe la kumutu kwanu adaliŵerenga lonse.
Choncho musati muziwopa ai. Ndinu a mtengo woposa atimba ambiri.
“Aliyense wondivomereza pamaso pa anthu, Inenso ndidzamuvomereza pamaso pa Atate anga amene ali Kumwamba.
Koma aliyense wondikana pamaso pa anthu kuti Ine sandidziŵa, Inenso ndidzamkana pamaso pa Atate anga amene ali Kumwamba kuti sindimdziŵa.
“Kodi mukuyesa kuti ndidadzapereka mtendere pansi pano? Sindidadzapereke mtendere ai, koma nkhondo.
Inetu paja ndidadzalekanitsa mwana wamwamuna ndi bambo wake, mwana wamkazi ndi mai wake, mkazi ndi apongozi ake aakazi,
mwakuti adani a munthu adzakhala a m'banja mwake omwe.
“Munthu wokonda bambo wake kapena mai wake koposa Ine, ngwosayenera kukhala wophunzira wanga. Ndipo wokonda mwana wake wamwamuna kapena wamkazi koposa Ine, ngwosayenera kukhala wophunzira wanga.
Amene sasenza mtanda wake ndi kumanditsata, ngwosayenera kukhala wophunzira wanga.
Munthu woyesa kusunga moyo wake, adzautaya, ndipo wotaya moyo wake chifukwa cha Ine, adzausunga.
Simoni, wa m'chipani chandale cha Azelote; ndiponso Yudasi Iskariote, amene pambuyo pake adapereka Yesu kwa adani ake.
Ophunzira khumi ndi mmodzi aja adapita ku Galileya kuphiri kumene Yesu adaapangana nawo kuti akakumane.
Pamene adamuwona, adampembedza, koma ena ankakayika.
Yesu adadza pafupi naŵauza kuti, “Mphamvu zonse zapatsidwa kwa Ine Kumwamba ndi pansi pano.
Nchifukwa chake inu pitani kwa anthu a mitundu yonse, mukaŵasandutse ophunzira anga. Muzikaŵabatiza m'dzina la Atate, ndi la Mwana ndi la Mzimu Woyera.
Mwadzidzidzi kudachita chivomezi chachikulu. Ndiye kuti mngelo wa Ambuye adaatsika kuchokera Kumwamba, nadzagubuduza chimwala chija, nkukhalapo.
Muzikaŵaphunzitsa kusunga zonse zimene Ine ndidakulamulani. Ndipo Ineyo ndili nanu masiku onse, mpaka kutha kwa dziko lino lapansi.”
Anali wofooka pamene adapachikidwa pa mtanda, komabe tsopano ali moyo mwa mphamvu ya Mulungu. Ifenso ndife ofooka mwa Iye, koma tidzakhala amoyo pamodzi naye ndi mphamvu ya Mulungu, pogwira ntchito yathu pakati panu.
Motero polalika sitidzilalika tokha, koma timalalika Yesu Khristu, kuti ndiye Ambuye. Ife ndife atumiki anu chabe chifukwa cha Yesuyo.
Ndife, Paulo ndi Timoteo, atumiki a Khristu Yesu. Tikulembera onse a mu mzinda wa Filipi, amene ali anthu ake a Mulungu mwa Khristu Yesu. Tikulemberanso oyang'anira Mpingo ndi atumiki ao.
Tsono adasankhapo khumi ndi aŵiri, naŵatcha dzina loti, “Atumwi.” Adaŵauza kuti, “Ndasankha inu kuti muzikhala nane, ndidzakutumani kukalalika,
Tsono adaŵauza kuti, “Pitani ku dziko lonse lapansi, kalalikireni anthu onse Uthenga Wabwino.
Ndine, Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwa kufuna kwa Mulungu. Ndili limodzi ndi Timoteo, mbale wathu.
Yakobe, Petro ndi Yohane, amene anthu ankaŵaona kuti ndi mizati mu Mpingo, adazindikira kuti ineyo Mulungu adandipatsadi ntchito imeneyi. Motero adagwirana chanza ndi ine ndiponso ndi Barnabasi, kutsimikiza chiyanjano chathu. Ndipo tidavomerezana kuti ine ndi Barnabasi tipite kwa anthu a mitundu ina, iwowo apite kwa Ayuda.
Ndife, Paulo, Silivano ndi Timoteo. Tikulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli wake wa Mulungu Atate, ndiponso wa Ambuye Yesu Khristu. Mulungu akukomereni mtima ndi kukupatsani mtendere.
Kutacha adaitana ophunzira ake, nasankhapo khumi ndi aŵiri. Adaŵatcha “atumwi.”
Anthu ake anali aŵa: Simoni (amene Yesu adamutcha dzina loti Petro) ndi mbale wake Andrea; Yakobe ndi Yohane; Filipo ndi Bartolomeo;
Mateyo ndi Tomasi; Yakobe (mwana wa Alifeyo) ndi Simoni (wa m'chipani chandale cha Azelote;)
Yudasi (mwana wa Yakobe) ndiponso Yudasi Iskariote (amene pambuyo pake adapereka Yesu kwa adani ake.)
Ndife, Paulo, Silivano ndi Timoteo. Tikulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli wake wa Mulungu Atate, ndiponso wa Ambuye Yesu Khristu.
Yesu adaŵauza kuti, “Ndithu ndikunenetsa kuti Mulungu akadzakonzanso zinthu zonse, Mwana wa Munthu adzakhala pa mpando wake wachifumu ndi waulemerero. Tsono inunso amene mudanditsatanu, mudzakhala pa mipando yachifumu khumi ndi iŵiri mukuweruza mafuko khumi ndi aŵiri a Aisraele.
Yesu adaitana ophunzira ake khumi ndi aŵiri aja naŵapatsa ulamuliro ndi mphamvu zotulutsira mizimu yoipa yonse ndi zochiritsira nthenda.
Pamene atumwi aja adabwerako, adafotokozera Yesu zonse zimene adaachita. Tsono Iye adaŵatenga nakakhala nawo paokha ku mudzi wina, dzina lake Betsaida.
Anthu ambirimbiri ataona zimenezi, adamtsatira. Iye adaŵalandira bwino nayamba kulankhula nawo za ufumu wa Mulungu, nkumachiritsa odwala.
Dzuŵa lili pafupi kuloŵa, ophunzira khumi ndi aŵiri aja adadzauza Yesu kuti, “Bwanji anthuŵa azinyamuka tsopano, apite ku midzi ndi ku miraga ili pafupiyi, kuti akapeze malo ogona ndiponso chakudya, chifukwatu kuno nkuthengo.”
Koma Yesu adaŵauza kuti, “Inuyo apatseni chakudya.” Iwo adati, “Tili ndi buledi msanu ndi nsomba ziŵiri zokha. Kaya kapena tipite tikaŵagulire anthu onseŵa chakudya?”
Ndiye kuti amuna okha adaalipo ngati zikwi zisanu. Tsono Yesu adauza ophunzira ake kuti, “Auzeni anthuŵa akhale pansi m'magulumagulu, gulu lililonse anthu ngati makumi asanu.”
Ophunzira aja adaŵakhalitsadi anthu onse aja pansi.
Pambuyo pake Yesu adatenga buledi msanu uja ndi nsomba ziŵiri zija, nayang'ana kumwamba, nkuthokoza Mulungu. Kenaka atanyemanyema bulediyo, adazipereka kwa ophunzira ake kuti agaŵire anthuwo.
Anthu onse aja adadya nakhuta. Ndipo ophunzira aja adatola zotsala, nkudzaza madengu khumi ndi aŵiri.
Nthaŵi ina pamene Yesu ankapemphera yekha, ophunzira ake adaali naye. Tsono Iye adaŵafunsa kuti, “Kodi anthu amati Ine ndine yani?”
Iwo adati, “Ena amati ndinu Yohane Mbatizi, ena amati ndinu Eliya. Koma enanso amati mneneri wina wakale wauka kwa akufa.”
Adaŵatuma kuti akalalike za ufumu wa Mulungu, ndi kukachiritsa anthu odwala.
Pambuyo pake Ambuye adasankha anthu 72, naŵatuma aŵiriaŵiri kuti atsogole kupita ku mudzi uliwonse ndi ku malo aliwonse kumene Iye ankati apiteko.
Ndine, Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu, monga adalamulira Mulungu, Mpulumutsi wathu, ndiponso Khristu Yesu, chiyembekezo chathu.
Si ndinutu mudandisankha Ine ai, koma ndine ndidakusankhani inu. Ndipo ndidakupatulani kuti mukabereke zipatso, zipatso zake zokhalitsa. Motero chilichonse chimene mungapemphe Atate potchula dzina langa, adzakupatsani.
Ndine, Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu, mwa kufuna kwa Mulungu. Adandituma kuti ndilalike chilonjezo cha moyo umene uli mwa Khristu Yesu.
Ndine, Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Adandituma kuti amene Mulungu adaŵasankha, ndiŵatsogolere ku chikhulupiriro, azizindikira choona chimene chimaŵafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu,
kufikira tsiku limene adatengedwa kupita Kumwamba. Mwa mphamvu ya Mzimu Woyera, anali atauza atumwi amene adaŵasankha aja zoti iwowo adzachite.
Koma mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera akadzabwera pa inu, ndipo mudzakhala mboni zanga ku Yerusalemu, ku Yudeya ndi ku Samariya konse, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
Nanga ife tingapulumuke bwanji tikapanda kusamala chipulumutso chachikulu chotere? Ambuye ndiwo amene adalankhula poyamba za chipulumutsochi, kenaka amene adamva mau aowo, adatitsimikizira kuti ndi oona.
Mulungu yemwe ankachitira umboni pakuchita zizindikiro, zinthu zozizwitsa ndi ntchito zamphamvu zamitundumitundu, ndi pakuŵagaŵira mphatso za Mzimu Woyera monga momwe Iye ankafunira.
Ndine, Yakobe, mtumiki wa Mulungu ndi wa Ambuye Yesu Khristu. Ndikupereka moni kwa inu anthu a Mulungu, a mafuko khumi ndi aŵiri, obalalikana ku maiko osiyanasiyana.
Ataloŵa mumzindamo, adakwera ku chipinda cham'mwamba kumene ankakhala: panali Petro, Yohane, Yakobe ndi Andrea; Filipo ndi Tomasi; Bartolomeo ndi Mateyo; Yakobe (mwana wa Alifeyo,) ndi Simoni (wa m'chipani chandale cha Azelote,) ndiponso Yudasi (mwana wa Yakobe.)
Onseŵa ankalimbikira kupemphera ndi mtima umodzi, pamodzi ndi akazi ena, ndi Maria amai ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
Ndine, Petro, mtumwi wa Yesu Khristu. Ndikulemba kalatayi kwa inu osankhidwa a Mulungu, amene muli obalalikira ku chilendo, ku maiko a ku Ponto, Galatiya, Kapadokiya, Asiya ndi Bitiniya.
Tsono adaŵachitira maere anthu aŵiriwo. Maerewo adagwera Matiasi, ndipo iyeyo adawonjezedwa pa gulu lija la atumwi khumi ndi mmodzi.
Tsopano ndili nawo mau akulu a mpingo amene ali pakati panu, ine mkulu mnzao. Ndinenso mboni ya zoŵaŵa za Khristu, ndipo ndikuyembekeza kudzalandira nao ulemerero umene uti udzaoneke.
Ndine, Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndikulemba kalatayi kwa anthu amene adalandira chikhulupiriro chomwe ifenso tidalandirako. Iwonso adachilandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.
Tsiku ndi tsiku ankasonkhana ndi mtima umodzi m'Nyumba ya Mulungu, ndipo ankadyera pamodzi kunyumba kwao. Ankadya chakudya chaocho mosangalala ndiponso ndi mtima waufulu.
Ankatamanda Mulungu, ndipo anthu onse ankaŵakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankaŵawonjezera ena olandira chipulumutso.
Tsiku lina Petro ndi Yohane ankapita ku Nyumba ya Mulungu pa 3 koloko madzulo, nthaŵi ya mapemphero.
Adamzindikira kuti ndi yemwe uja amene ankakhala pa Khomo Lokongola la Nyumba ya Mulungu. Ndipo adazizwa ndithu ndi kudabwa ndi zimene zidamchitikira.
Tikukulemberani za Iye uja amene adaalipo kuyambira pa chiyambi, amene tidamumva ndipo tidamuwona ndi maso athu, amene tidampenya ndithu, ndipo tidamkhudza ndi manja athu: Iyeyo ndiye Mau opatsa moyo.
Tikanena kuti sitidachimwe, tikumuyesa wonama Mulungu, ndipo mau ake sali mwa ife.
Moyowo udaoneka, ndipo ife tidauwona. Tikuuchitira umboni, ndipo tikukulalikirani za moyo wosatha, umene unali kwa Atate ndipo udatiwonekera.
Chimene tidachiwona ndi kuchimva, tikukulalikirani, kuti inunso mukhale a mtima umodzi ndi ife. Kuyanjana kwathu tikuyanjana ndi Atate, ndiponso ndi Mwana wao, Yesu Khristu.
Ine mkulune ndikulemba kalatayi kwa mai wosankhidwa ndi Mulungu, ndi kwa ana ake amene ndimaŵakonda kwenikweni. Ndipo sindine ndekha amene ndimakukondani, komanso onse odziŵa choona.
Atumwi ankachita zizindikiro ndi zozizwitsa zambiri pakati pa anthu. Onse okhulupirira Khristu ankasonkhana ndi mtima umodzi m'Khonde la Solomoni.
Mwa anthu enawo panalibe ndi mmodzi yemwe amene adaalimba mtima kuti azisonkhana nawo, komabe anthu onse ankaŵatama.
Ndipo anthu okhulupirira Ambuye ankachulukirachulukira, mwakuti linali ndithu gulu lalikulu la amuna ndi akazi omwe.
Tsono anthu ankatulutsira odwala ao m'miseu yamumzinda, nkumaŵagoneka pa mabedi ndi pa mphasa, kuti Petro podutsapo, chithunzithunzi chake chokha ena mwa iwo chiŵafike.
Kunkasonkhananso anthu ochuluka ochokera ku midzi yozungulira Yerusalemu. Anali atanyamula anthu odwala, ndiponso ena osautsidwa ndi mizimu yoŵaipitsa. Onsewo ankachiritsidwa.
Tsono atumwi khumi ndi aŵiri aja adasonkhanitsa gulu lonse la ophunzira, naŵauza kuti, “Sibwino kuti ife tizisiya kulalika mau a Mulungu nkumayang'anira za chakudya.
Nchifukwa chake abale, pakati panupa sankhanipo amuna asanu ndi aŵiri, a mbiri yabwino, odzazidwa ndi Mzimu Woyera ndiponso ndi nzeru. Tidzapatsa iwowo ntchitoyi.
Koma ife tidzadzipereka ku ntchito ya kupemphera ndi kulalika mau a Mulungu.”
Akuti: Ntchito zanu zonse ndikuzidziŵa. Ndikudziŵa kuti mwakhala mukugwira ntchito kolimba, ndipo kuti muli ndi kupirira kosatepatepa. Ndikudziŵanso kuti anthu ochimwa simungaŵalekerere. Anthu amene amadzitcha atumwi, pamene sali atumwi konse, mwaŵayesa, ndipo mwaŵapeza kuti ngonama.
Linga la mzindawo lidaamangidwa pa maziko khumi ndi aŵiri, ndipo pamazikopo padaalembedwa maina a atumwi khumi ndi aŵiri a Mwanawankhosa uja.
Pamene atumwi okhala ku Yerusalemu adamva kuti anthu a ku Samariya alandira mau a Mulungu, adatumako Petro ndi Yohane.
Koma Ambuye adamuuza kuti, “Pita, pakuti iyeyu ndi mtumiki wanga amene ndidamsankha kuti akalalikire dzina langa anthu a mitundu ina, mafumu, ndiponso Aisraele.
Sadaonekere kwa anthu onse ai, koma kwa mboni zimene Mulungu adazisankhiratu. Ndiye kuti adaonekera kwa ife, amene tinkadya ndi kumwa naye pamodzi atauka kwa akufa.
“Inu ndinu amene mwakhala ndi Ine pa masautso anga onse.
Nchifukwa chake, monga Atate anga adandipatsa ufumu, Inenso ndikukupatsani ufumu.
Tsono Satana adamuloŵa Yudasi wotchedwa Iskariote, amene anali mmodzi mwa ophunzira khumi ndi aŵiri aja a Yesu.
Ndikadzaloŵa mu ufumu wanga, muzidzadya ndi kumwa pamodzi nane, ndipo mudzakhala pa mipando yachifumu nkumaweruza mafuko khumi ndi aŵiri a Israele.”
Yesu adatinso, “Mtendere ukhale nanu. Monga Atate adandituma, Inenso ndikukutumani.”
Pambuyo pake adaŵauzira mpweya nati, “Landirani Mzimu Woyera.
Atumwi aja, ndiponso abale onse amene anali ku Yudeya, adamva kuti anthu a mitundu ina nawonso alandira mau a Mulungu.
Pamene Petro adaona zimenezi, adalankhula nawo anthuwo, adati, “Inu Aisraele, bwanji mukuzizwa ndi zimenezi? Bwanji mukutiyang'ana ngati kuti tamuyendetsa munthuyu ndi mphamvu zathuzathu? Kodi mukuyesa kuti nchifukwa choti ndife opembedza Mulungu kopambana?
Mpingo wa ku Yerusalemu utamva zimene zidachitikazo, udatuma Barnabasi ku Antiokeyako.
Pamene iye adafika kumeneko nkuwona m'mene Mulungu adaŵadalitsira, adakondwa, nalimbikitsa onsewo kuti atsimikize mtima kukhala okhulupirika kwa Ambuye.
Barnabasiyo anali munthu wolungama, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera ndi chikhulupiriro. Choncho anthu ambirimbiri adakopeka nadzipereka kwa Ambuye.
Pafupi ngati nthaŵi imeneyo mfumu Herode adagwira ena a mu Mpingo kuti aŵazunze.
Onsewo adapitirira gulu loyamba la asilikali aja, kenaka lachiŵiri, mpaka kukafika pa chitseko chachitsulo cha pa chipata choloŵera mu mzinda. Chitsekocho chidangodzitsekukira chokha, iwowo nkutuluka. Adayenda ndithu mu mseu wina wamumzindamo. Atafika polekezera pake mngelo uja adamchokera.
Pamenepo Petro adadzidzimuka nati, “Tsopano ndikudziŵadi kuti Ambuye anatuma mngelo wao ndipo andipulumutsa kwa Herode, ndi ku zoipa zonse zimene Ayuda ankayembekeza kuti zidzandichitikira.”
Atazindikira zimenezi, adapita kunyumba kwa Maria, amai ake a Yohane wotchedwanso Marko. Anthu ambiri anali atasonkhana kumeneko akupemphera.
Pamene Petro adagogoda pa chitseko chapakhomo, mtsikana wina, dzina lake Roda, adabwera kuti amtsekulire.
Atazindikira liwu lake kuti ndi la Petro, adakondwa kwambiri, kotero kuti sadatsekule chitsekocho, koma adathamangiranso m'kati nakawuza ena aja kuti, “Petro ali pakhomopa!”
Anthuwo adati, “Wapenga iwe!” Koma iye adalimbikira kuti nzoonadi. Apo iwo adati, “Ndi mngelo wake ameneyo.”
Koma Petro ankangogogodabe. Pamene adamtsekulira nkuwona kuti ndiyedi, adangoti kakasi.
Petro adakweza dzanja kuti iwo akhale chete, naŵafotokozera m'mene Ambuye adaamtulutsira m'ndende muja. Ndipo adati, “Mumuuze Yakobe ndi abale ena aja zimenezi.” Pamenepo iye adatuluka napita kwina.
Kutacha, asilikali aja adasokonezeka kwabasi nati, “Petro wapita kuti?”
Herode adamufunafuna, koma osampeza. Adaŵazenga mlandu alonda aja, nalamula kuti aphedwe. Pambuyo pake Herode adachoka ku Yudeya kupita ku Kesareya, nakakhala kumeneko.
Adalamula kuti Yakobe, mbale wake wa Yohane, aphedwe ndi lupanga.
Petro, atadzazidwa ndi Mzimu Woyera, adaŵayankha kuti, “Inu atsogoleri ndi akuluakulu muli apa,
Mu mpingo wa ku Antiokeya munali alaliki ndi aphunzitsi aŵa: Barnabasi, Simeoni (wotchedwa Wakuda), Lusio wa ku Kirene, Manaene (amene adaaleredwa pamodzi ndi bwanamkubwa Herode), ndiponso Saulo.
nati, “Iwe mwana wa Satana, mdani wa chilungamo, wa mtima wa kunyenga kulikonse ndi kuchenjeretsa kwamtundumtundu, udzaleka liti kupotoza njira zolungama za Ambuye?
Ona dzanja la Ambuye likukantha tsopano apa. Ukhala wakhungu osaonanso dzuŵa pa kanthaŵi.” Nthaŵi yomweyo khungu ndi mdima zidamgweradi, ndipo adayamba kufunafuna anthu oti amgwire dzanja ndi kumtsogolera.
Pamene bwanamkubwa uja adaona zimene zidachitikazo, adakhulupirira. Adaadabwa nazo zimene iwo adaaphunzitsa za Ambuye.
Paulo ndi anzake adayenda m'chombo kuchokera ku Pafosi kukafika ku Perga m'dera la Pamfiliya. Koma Yohane adaŵasiya nabwerera ku Yerusalemu.
Kuchokera ku Perga iwo adapitirira nakafika ku Antiokeya m'dera la Pisidiya. Pa tsiku la Sabata adaloŵa m'nyumba yamapempherero ya Ayuda, nakhala pansi.
Ataŵerengedwa mau a m'buku la Malamulo a Mose ndi m'buku la aneneri, akulu a nyumba yamapemphero ija adaŵatumira mau oŵauza kuti, “Abale, ngati muli ndi mau olimbikitsa nawo anthuŵa, nenani.”
Apo Paulo adaimirira nakweza dzanja kuti anthu akhale chete, ndipo adayamba kulankhula. Adati, “Inu Aisraele, ndi ena nonse oopa Mulungu, mverani.
Mulungu wa mtundu wathu wa Aisraele, adasankha makolo athu, ndipo adaŵakuza pamene anali alendo ku dziko la Ejipito. Adaŵatulutsa m'dzikomo ndi dzanja lake lamphamvu,
adaŵasamalabe mopirira m'chipululu zaka makumi anai.
Iye adaononga mitundu isanu ndi iŵiri ya anthu m'dziko la Kanani, napereka dziko lao kwa Aisraele kuti likhale laolao. Zonsezi zidatenga zaka ngati 450.
Tsiku lina pamene iwo adasonkhana kuti apembedze Ambuye ndi kuti asale zakudya, Mzimu Woyera adaŵauza kuti, “Mundipatulire Barnabasi ndi Saulo kuti akagwire ntchito imene ndaŵaitanira.”
“Pambuyo pake adaŵapatsa oweruza kufikira nthaŵi ya mneneri Samuele.
Kenaka anthu adapempha kuti aŵapatse mfumu, ndipo Mulungu adaŵapatsa Saulo, mwana wa Kisi, munthu wa fuko la Benjamini, iye nkuŵalamulira pa zaka makumi anai.
Pambuyo pake Mulungu adamchotsa Sauloyo, naika Davide kuti akhale mfumu yao. Za iyeyu Mulungu adanena kuti, ‘Ndapeza Davide, mwana wa Yese, ndiye munthu wanga wapamtima, amene adzachita zonse zimene Ine ndifuna.’
Mwa zidzukulu za Davideyo Mulungu adasankha Yesu kuti akhale Mpulumutsi wa Aisraele, monga momwe adaalonjezera kale.
Iyeyo asanayambe ntchito, Yohane ankalalikira Aisraele onse kuti atembenuke mtima ndi kubatizidwa.
Pamene Yohane anali pafupi kutsiriza ntchito yake, adafunsa anthu kuti, ‘Kodi inu mumayesa kuti ine ndine yani? Inetu sindine amene mukumuyembekezayo ai. Koma pakubwera wina pambuyo panga amene ine sindili woyenera ngakhale kumvula nsapato zake.’
“Ine abale, zidzukulu za Abrahamu, ndi ena nonse oopa Mulungu, uthenga wa chipulumutsowu Mulungu watumizira ife.
Anthu okhala ku Yerusalemu ndi akulu ao sadamzindikire Yesu, ndipo sadamvetse mau a aneneri amene amaŵerengedwa tsiku la Sabata lililonse. Komabe pakumzenga mlandu Yesuyo kuti aphedwe, adachitadi zimene aneneri adaaneneratu.
Ngakhale sadapeze konse chifukwa chomuphera, komabe adapempha Pilato kuti Yesuyo aphedwe.
Ndipo atachita zonse zimene zidalembedwa za Iye, adamtsitsapo pa mtanda paja namuika m'manda.
Tsono atasala zakudya ndi kupemphera adaŵasanjika manja naŵatuma.
Koma pamene atumwi aja, Barnabasi ndi Paulo, adamva zimenezi, adang'amba zovala zao, nathamangira pakati pa anthuwo. Adalankhula mokweza mau kuti,
Koma Petro ndi atumwi enawo adati, “Tiyenera kumvera Mulungu koposa kumvera anthu.
Koma Petro adamufunsa kuti, “Iwe Ananiya, chifukwa chiyani walola mtima wako kugwidwa ndi Satana mpaka kumanamiza Mzimu Woyera pakupatula ndalama zina za munda wako?
Mulungu wa makolo athu adaukitsa Yesu kwa akufa, Iye amene inu mudaamupha pakumpachika pa mtanda.
Ameneyo Mulungu adamkweza ku dzanja lake lamanja kuti akhale Mtsogoleri ndi Mpulumutsi. Adachita zimenezi kuti apatse Aisraele mwai wotembenuka mtima kuti machimo ao akhululukidwe.
Mboni za zimenezi ndi ifeyo ndiponso Mzimu Woyera amene Mulungu adampereka ngati mphatso kwa anthu omvera Iye.”
Koma Paulo ndi Barnabasi adatsutsana nawo kolimba. Tsono abale adapangana kuti Paulo ndi Barnabasi, ndi abale ena a ku Antiokeya, apite ku Yerusalemu kukakambirana ndi atumwi ndi akulu a mpingo za nkhaniyi.
Simoni uja ataona kuti Mzimu Woyera waperekedwa kwa iwo atumwi aja ataŵasanjika manja, adafuna kuŵapatsa ndalama atumwiwo.
Adati, “Bwanji mutandipatsako inenso mphamvu imeneyi, kuti aliyense amene ndikamsanjike manja, akalandire Mzimu Woyera.”
Anthu ena okonda Mulungu adakaika maliro a Stefano namlira kwambiri.
Petro adamuyankha kuti, “Ndalama zakozo ukatayike nazo pamodzi. Iwe ukuganiza kuti ungathe kupata mphatso ya Mulungu pakupereka ndalama kodi?
Ulibe gawo kapena malo pa ntchito imeneyi, pakuti mtima wako suli wolungama pamaso pa Mulungu.
Pamene Petro ankati aziloŵa, Kornelio adadzakumana naye, nadzigwetsa kumapazi kwake, namuŵeramira.
Koma Petro adamuimiritsa nati, “Iyai, imirirani, inenso ndine munthu chabe.”
Pamene ankadutsa m'mizinda, ankadziŵitsa anthu mfundo zimene atumwi ndi akulu a mpingo a ku Yerusalemu aja adaapanga, nkumaŵauza kuti azisunge.
Paulo ndi Silasi atatuluka m'ndende muja adapita kunyumba kwa Lidia. Kumeneko adaonana ndi abale, ndipo ataŵalimbikitsa, adachoka.
Motero mipingo ya akhristu inkamangidwa pa chikhulupiriro cholima, ndipo oloŵamo ankachulukirachulukira tsiku ndi tsiku.
Mzimu Woyera anali atandiwuza kuti ndisakayike konse, koma ndipite nawo. Abale asanu ndi mmodzi aŵa nawonso adandiperekeza, ndipo tidakaloŵa m'nyumba ya Kornelio.
Myuda wina, dzina lake Apolo, mbadwa ya ku Aleksandriya, adabwera ku Efeso. Anali munthu wodziŵa kulankhula ndi wodziŵa Malembo kwambiri.
Iyeyu adaaphunzitsidwa Njira ya Ambuye, ndipo ndi changu chachikulu ankalankhula ndi kuphunzitsa za Yesu molongosoka, chonsecho ankangodziŵa za ubatizo wa Yohane wokha.
Tsono adayamba kulankhula molimba mtima m'nyumba yamapemphero ya Ayuda. Koma pamene Prisila ndi Akwila anamumva, adamtenga namufotokezera Njira ya Mulungu molongosoka koposa.
Anthu ena ochokera ku Yudeya adabwera ku Antiokeya, namaphunzitsa abale kuti, “Ngati simuumbala potsata mwambo wa Mose, simungathe kupulumuka.”
Tsono mukumuyeseranji Mulungu pakuika m'khosi mwa ophunzirawo goli limene ngakhale makolo athu kapena ife tomwe tidalephera kulisenza?
Iyai, timakhulupirira kuti chopulumutsa iwowo, ndi ife tomwe, ndi kukoma mtima kwa Ambuye Yesu.”
Onse mumsonkhanomo adangoti chete nkumamvetsera Barnabasi ndi Paulo akufotokoza za m'mene Mulungu adachitira zizindikiro ndi zozizwitsa pakati pa akunja kudzera mwa iwowo.
Pamene iwo aja adatha kulankhula, Yakobe adati, “Abale anga, mundimvere.
Simoni wafotokoza za m'mene Mulungu pachiyambi pomwe adakumbukira anthu a mitundu ina, pa kupatula ena pakati pao kuti akhale anthu akeake.
Zimenezi zikuvomerezana ndi mau a aneneri. Paja kudalembedwa kuti,
“ ‘Zitatha zimenezi ndidzabwerera, ndidzamanganso nyumba ya Davide imene idagwa. Ndidzamanganso zopasuka zake, ndi kuikonzanso.
Ndidzachita choncho kuti anthu ena onse afunefune Ambuye, ndiye kuti, anthu a mitundu yonse amene amadziŵika ndi dzina langa.
Akutero ndi Chauta amene adaulula zimenezi kuyambira kalekale.’
“Nchifukwa chake ine ndikuti, tisaŵavute anthu a mitundu ina amene akutembenuka mtima nkumatsata Mulungu.
Koma Paulo ndi Barnabasi adatsutsana nawo kolimba. Tsono abale adapangana kuti Paulo ndi Barnabasi, ndi abale ena a ku Antiokeya, apite ku Yerusalemu kukakambirana ndi atumwi ndi akulu a mpingo za nkhaniyi.
Tsono titasonkhana, tavomerezana kusankha anthu ndi kuŵatuma kwa inu. Adzabwera pamodzi ndi okondedwa athu Barnabasi ndi Paulo.
Amene adadzipereka kuti atumikire Ambuye athu Yesu Khristu.
Nchifukwa chake tatuma Yudasi ndi Silasi kuti adzakufotokozereni pakamwa zimene talemba m'kalatayi.
Pamene Apolo anali ku Korinto, Paulo adayendera maiko apamtunda, nakafika ku Efeso. Kumeneko adapezako ophunzira ena,
Paulo ali ku Mileto, adatumiza mau ku Efeso kuitana akulu a mpingo.
Iwo atafika, adaŵauza kuti, “Inu nomwe mukudziŵa m'mene ndidakhalira nanu masiku onse, kuyambira tsiku loyamba lija ndidafika ku Asiya.
Iyeyo adayamba kutitsatira Paulo ndi ife, akufuula kuti, “Anthu aŵa ndi atumiki a Mulungu Wopambanazonse, akukulalikirani njira ya chipulumutso.”
Tsopano ndifuna kukuuzani kanthu, inu amene simuli Ayuda. Malinga nkuti ndine wotumidwa kwa anthu a mitundu ina, ndimaunyadira utumiki wanga umenewu.
M'thupi lathu limodzi lomweli tili ndi ziwalo zambiri, ndipo ziwalozo zili ndi ntchito zosiyanasiyana.
Momwemonso ife, ngakhale tili ambiri, ndife thupi limodzi, olumikizana mwa Khristu, ndipo tonse, aliyense pa mbali yake, ndife ziwalo zolumikizana.
pakundipatula kuti ndikhale mtumiki wa Khristu Yesu kwa anthu a mitundu ina. Adandipatsa ntchito yolalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu ngati wansembe, kuti anthuwo akhale ngati nsembe yokomera Iye ndi yoperekedwa mwa Mzimu Woyera.
Ndine, Paulo, amene mwa kufuna kwa Mulungu ndidaitanidwa kuti ndikhale mtumwi wa Khristu Yesu. Ndili pamodzi ndi mbale wathu, Sostene.
Kodi Apolo nchiyani? Paulonso nchiyani? Ndi atumiki chabe a Mulungu, amene adakufikitsani ku chikhulupiriro. Aliyense adangogwira ntchito imene Mulungu adampatsa.
Kodi sindine mfulu? Kodi sindine mtumwi? Kodi suja ine ndidamuwona Yesu Ambuye athu? Kodi suja inu ndinu zipatso za ntchito yanga yogwirira Ambuye?
Koma chifukwa chakuti Mulungu adandikomera mtima, ndili monga ndilirimu. Ndipo kukoma mtima kwakeko sikunali kopanda phindu, popeza kuti ndidagwira ntchito koposa atumwi ena onse. Komabe si ndine ndidaigwira, koma mphamvu za Mulungu zimene zikundilimbikitsa.
Inetu ndine wamng'onong'onodi mwa atumwi onse. Sindine woyenera konse kuti ndizitchedwa mtumwi, pakuti ndinkazunza Mpingo wa Mulungu.
Tsono ndife akazembe oimirira Khristu, ndipo kudzera mwa ifeyo Mulungu mwini ndiye akulankhula nanu mokudandaulirani. Tikukupemphani m'dzina la Khristu kuti muvomere kuyanjananso ndi Mulungu.
Abale, ntakuuzani: Uthenga Wabwino umene ine ndimalalika, ndi wosachokera kwa anthu.
Sindidaulandire kwa munthu, ndipo palibenso munthu amene adandiphunzitsa Uthengawo, koma ndi Yesu Khristu yemwe amene adawuulula kwa ine.
Ndine, Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwa kufuna kwa Mulungu. Ndili limodzi ndi mbale wathu Timoteo. Tikulembera mpingo wa Mulungu umene uli ku Korinto, ndiponso anthu onse a Mulungu okhala m'dziko lonse la Akaiya.
Makamaka adaaona kuti Mulungu adandipatsa ine ntchito ya kulalika Uthenga Wabwino kwa anthu osakhala Ayuda, monga momwe adapatsira Petro ntchito ya kuulalika kwa Ayuda.
Pakuti Mulungu yemweyo amene adagwira ntchito mwa Petro pomutuma ngati mtumwi kwa Ayuda, adagwiranso ntchito mwa ine, pondituma ngati mtumwi kwa anthu a mitundu ina.
Ndiyeneradi kuthokoza chifukwa mwakhala mukugwirizana nane ndi kundithandiza kufalitsa Uthenga Wabwino, kuchokera tsiku limene mudayamba kukhulupirira mpaka tsopano.
Akutinso moni Yesu, wotchedwa Yusto. Mwa ochokera ku Chiyuda ndi atatu okhaŵa amene akundithandiza pa ntchito ya Ufumu wa Mulungu, ndipo andilimbikitsa kwambiri.
Koma timalalika chifukwa Mulungu adativomereza natisungiza Uthenga Wabwino kuti tiulalike. Choncho tikamaphunzitsa sitifuna kukondweretsa anthu, koma timafuna kukondweretsa Mulungu, amene amapenyetsetsa mitima yathu.
Tsono abale, khalani olimbika, ndipo mugwiritse miyambo imene tidakuphunzitsani ndi mau apakamwa kapena am'makalata.
Uzimenya nkhondo yabwino ya kusunga chikhulupiriro, mpaka ukalandire moyo wosatha. Paja Mulungu adakuitanira zimenezi, ndipo udavomera bwino chikhulupiriro chako pamaso pa mboni zambiri.
Mau amene udamva kwa ine pamaso pa mboni zambiri, uŵasungitse anthu okhulupirika amene adzathe kuŵaphunzitsanso kwa ena.
Uziŵakumbutsa anthu onse kuti azigonjera akulu oweruza ndi olamulira. Aziŵamvera ndipo azikhala okonzeka kuchita ntchito iliyonse yabwino.
Muzikumbukira atsogoleri anu amene ankakulalikirani mau a Mulungu. Muzilingalira za moyo wao ndi m'mene adafera, ndipo muzitsanzira chikhulupiriro chao.
Koma inu ndinu fuko losankhidwa, ansembe achifumu, mtundu wopatulika, anthu akeake a Mulungu. Adakusankhani kuti mukalalike ntchito zamphamvu za Iye amene adakuitanani kuti mutuluke mu mdima, mukaloŵe m'kuŵala kwake kodabwitsa.
Aliyense mphatso imene adalandira kwa Mulungu azitumikira nayo anzake. Mukhale ngati akapitao ogwiritsa bwino ntchito mphatso zamitundumitundu zochokera kwa Mulungu.
Chimene tidachiwona ndi kuchimva, tikukulalikirani, kuti inunso mukhale a mtima umodzi ndi ife. Kuyanjana kwathu tikuyanjana ndi Atate, ndiponso ndi Mwana wao, Yesu Khristu.
Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, koma amaonjezerapo zina, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsocho, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana.
Tsono ife tiyenera kumaŵathandiza anthu otere, kuti tigwirizane nawo pa ntchito yofalitsa choona.
Ndi oti wanzeru akaŵamva, aonjezere kuphunzira kwake, ndipo munthu womvetsa zinthu apate luso,
Chachikulu pa nzeru ndi ichi: Kaya nchiyani chimene ungapate, peza nzeruyo, usalephere kupata khalidwe la kumvetsa zinthu.
“Inu ndinu kuŵala kounikira anthu onse. Mudzi wokhala pamwamba pa phiri sungabisike.
Munthu sati akayatsa nyale, nkuivundikira ndi mbiya. Koma amaiika pa malo oonekera, ndipo imaunikira anthu onse amene ali m'nyumbamo.
Chomwechonso inuyo muziwonetsa kuŵala kwanu pamaso pa anthu, kuti ataona ntchito zanu zabwino azilemekeza Atate anu akumwamba.
Yesu adaitana ophunzira ake khumi ndi aŵiri aja naŵapatsa ulamuliro ndi mphamvu zotulutsira mizimu yoipa yonse ndi zochiritsira nthenda.