Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

102 Mau a m'Baibulo Okhudza Moyo Wautali

Umoyo wautali, ndiwo umene tonse timaufuna. Kukhala ndi moyo wathanzi komanso wokhalitsa, ndicho chikhumbo cha Mulungu kwa ife kuyambira kale. Mukalowa m’buku la Genesis, muona kuti chifukwa cha imfa ndi kusamvera Mulungu ndi kuchimwa.

Koma Mulungu watipatsa lonjezo la moyo wautali. Mu Ekisodo 20:12, Mulungu akutiuza, "Lemekeza atate wako ndi amayi ako, kuti masiku ako akhale ochuluka m'dziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa." Ulemu kwa makolo athu ndi njira imodzi yopezera madalitso a moyo wautali.

Solomoni, munthu wanzeru, anatipatsanso malangizo abwino mu Eclesiastes. Iye anati, "Usachite zoipa zambiri, ndipo usakhale wopusa; ufera chiyani nthawi isanakwane? Ukatalikirana ndi zoipa, udzakhala ndi moyo wautali padziko lapansi." Kutalikirana ndi zoipa ndi njira ina yopezera moyo wautali.

Ndiponso, tiyenera kusamalira matupi athu, chifukwa ndiwo akachisi a Mulungu. Pali anthu ena amene Yesu sanawaitane kuti abwere kwa Iye, koma anawatenga kupita kumwamba. Mwina kusasamala matupi awo kunawapangitsa kuti afe msanga. Ndikofunika kuti tisamalire thanzi lathu.

Mulungu watipatsa malangizo ambiri m’Baibulo, ndipo ndi bwino kuwatsatira. Tiyeni tilemekeze makolo athu, tisamalire matupi athu, titalikirane ndi zoipa ndi kupusa, ndipo tipemphe nzeru kwa Mulungu. Tikamachita izi, tidzakhala ndi moyo wautali umene Mulungu amatifulira.


Masalimo 23:6

Zoonadi, zokoma zanu ndi chikondi chanu zidzakhala ndi ine masiku onse a moyo wanga. Ndidzakhala m'Nyumba mwanu moyo wanga wonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:18-19

Chauta amasamalira moyo wa anthu angwiro, ndipo choloŵa chao chidzakhalapo mpaka muyaya.

Pa nthaŵi ya mavuto sadzazunzika, pa nthaŵi yanjala, adzakhala nazo zakudya zochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 5:33

Muziyenda m'njira imene Chauta, Mulungu wanu, wakulamulani, kuti zinthu zidzakuyendereni bwino, ndipo mudzapitirire kukhala ndi moyo m'dziko limene mukakhalemolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:16

Ndidzampatsa moyo wautali ndi kumpulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 128:1-2

Ngwodala aliyense woopa Chauta, amene amayenda m'njira zake.

Udzadya zimene manja ako adagwirira ntchito. Udzasangalala, ndipo zinthu zidzakuyendera bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:2

Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka, ndipo udzakhala ndi moyo wabwino kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 9:11

Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo ndidzaonjezera zaka pa moyo wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 65:20

Ana sadzafanso ali akhanda, ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zao zonse. Amene adzafe ali a zaka zana limodzi zokha adzaoneka ngati anyamata. Kufa zisanakwane zaka zana limodzi kudzasonyeza kutembereredwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:27

Ndani mwa inu ndi maganizo ankhaŵa angathe kuwonjezera ngakhale tsiku limodzi pa moyo wake?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:93

Sindidzaiŵala konse malangizo anu, pakuti mwandipatsa nawo moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 2:6

Chauta amadzetsa imfa ndipo amabwezeranso moyo, amatsitsira ku manda, ndipo amaŵatulutsakonso.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 16:11

Mumandiwonetsa njira ya ku moyo. Ndimapeza chimwemwe chachikulu kumene kuli Inu, ndidzasangalala mpaka muyaya ku dzanja lanu lamanja.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:16

Maso anu adandiwona ndisanabadwe. Masiku a moyo wanga mudaŵalemberatu m'buku mwanu, asanayambe nkuŵerengedwa komwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:1-2

Mwana wanga, usaiŵale malangizo angaŵa, koma mtima wako usunge malamulo anga.

Ukatero, nkhokwe zako zidzadzaza ndi dzinthu dzambiri, mbiya zako zidzachita kusefukira ndi vinyo.

Mwana wanga, usanyoze malango a Chauta, usatope nako kudzudzula kwake.

Paja Chauta amadzudzula yemwe amamkonda, monga momwe atate amamchitira mwana wokondwera naye.

Ngwodala munthu amene wapeza nzeru, amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,

pakuti phindu la nzeru nloposa phindu la siliva, nloposanso ndi phindu la golide lomwe.

Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali. Palibe chinthu chochilakalaka cholingana ndi nzeruyo.

Ndi nzeru imene imakupatsa moyo wautali. Ndi nzeru imene imakuninkha chuma ndi ulemu.

Nzeru imakudzeretsa m'njira za chisangalalo, nimakuyendetsa mumtendere mokhamokha.

Nzeru ili ngati mtengo woŵapatsa moyo oigwiritsa. Ngodala amene amaikangamira molimbika.

Pamene adakhazikitsa dziko lapansi, Chauta adaonetsa nzeru. Pamene adakhazikitsa zakumwamba, adaonetsa nzeru za kumvetsa bwino.

Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka, ndipo udzakhala ndi moyo wabwino kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 25:7-8

Abrahamu adakhala ndi moyo zaka 175.

Adamwalira ali nkhalamba yotheratu, atagonera zaka zochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:14-15

Pakuti amene amandikangamira Ine Mulungu mwachikondi, ndidzampulumutsa. Ndidzamteteza popeza kuti amadziŵa dzina langa.

Akadzandiitana, ndidzamuyankha, ndidzakhala naye pa nthaŵi yamavuto. Ndidzamlanditsa ndi kumlemekeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:27

Kuwopa Chauta kumatalikitsa moyo, koma zaka za anthu oipa zidzachepa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 5:26

Udzafika ku manda utakalamba, monga m'mene zokolola zimachera pa nyengo yake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 71:18

Choncho Inu Mulungu, musandisiye ndekha ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbu, mpaka nditalalika mphamvu zanu kwa mibadwo yonse yakutsogolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 55:23

Koma Inu Mulungu mudzaŵaponya adani anga m'dzenje lozama lachiwonongeko. Anthu okhetsa magazi ndi onyenga sadzafika ngakhale theka la masiku ao. Koma ine ndidzadalira Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:10

Paja mau a Mulungu akuti. “Yemwe afuna kukondwera ndi moyo, ndi kuwona masiku abwino, aletse lilime lake kulankhula zoipa, ndiponso milomo yake kunena mabodza.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:30

Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imaoletsa mafupa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:14

Pakuti amene amandikangamira Ine Mulungu mwachikondi, ndidzampulumutsa. Ndidzamteteza popeza kuti amadziŵa dzina langa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 146:3-4

Musakhulupirire mafumu kapena anthu ena amene sangathe kuthandiza.

Pamene mpweya wa munthu uchokeratu, munthuyo amabwerera ku dothi, zimene ankafuna kuchita, zimatha tsiku lomwelo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:7-8

Usamadziwona ngati wanzeru. Uziwopa Chauta, ndipo uleke zoipa.

Kuchita choncho kudzapatsa thupi lako moyo, kudzalimbitsa mafupa ako.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 11:21

Pamenepo inu ndi ana anu, mudzakhala ndi moyo nthaŵi yaitali m'dziko limene Chauta, Mulungu wanu, adalumbira kuti adzapatsa makolo anu. Mudzakhala m'dziko limenelo nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 92:14

Mitengoyi imabalabe zipatso ngakhale itakalamba, nthaŵi zonse imakhala ndi madzi ndipo imabiriŵira,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:24

Njira yopita ku moyo imakamufikitsa ku ntchito zangwiro, kuti alewe malo a anthu akufa kunsiko.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 6:3

Tsono Chauta adati, “Sindidzalola anthu kukhala ndi moyo mpaka muyaya, popeza kuti munthu ndi thupi limene limafa. Kuyambira tsopano adzangokhala zaka 120.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:165

Anthu okonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, palibe china chotha kuŵagwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 78:70-72

Mulungu adasankhula Davide mtumiki wake, ndipo adakamtenga ku makola a nkhosa.

Adamtenga kumene ankaŵeta nkhosa zimene zinali ndi ana, kuti adzakhale mbusa wa Yakobe, fuko lake, wa Israele, choloŵa chake.

Davide adaŵasamala ndi mtima wolungama, naŵatsogolera ndi dzanja lake mwaluso.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 46:4

Mpaka mudzakalambe ndidzakhalabe Yemwe uja, mpaka mudzamere imvi ndidzakusamalani ndithu. Ndidakulengani, ndipo ndidzakunyamulani. Ndidzakusenzani ndipo ndidzakuwombolani.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:35-36

Paja wondipeza ine, wapeza moyo, ndipo amapeza kuyanja pamaso pa Chauta.

Koma wosandipeza ine, akudzipweteka ameneyo. Onse odana ndi ine, ngokonda imfa amenewo.”

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 7:17

Usachite kunyanyanso kuipa, usanyanye nawonso uchitsiru. Nanga uferenji nthaŵi yako isanakwane?

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:31

Imvi zili ngati chisoti chaufumu chopatsa ulemerero, munthu amazipata akakhala ndi moyo wautali.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 107:17-18

Ena adadwala chifukwa cha njira zao zoipa, nazunzika chifukwa cha machimo ao.

Sankafuna chakudya cha mtundu uliwonse, ndipo adayandikira ku zipata za imfa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:15-16

Kunena za munthu, masiku ake sakhalitsa, ali ngati a udzu, munthuyo amakondwa ngati duŵa lakuthengo.

Koma mphepo ikaombapo, duŵalo pamakhala palibe, siliwonekanso pa malo ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:7

Chachikulu pa nzeru ndi ichi: Kaya nchiyani chimene ungapate, peza nzeruyo, usalephere kupata khalidwe la kumvetsa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 58:11

Tsono ndidzakutsogolerani nthaŵi zonse, ndi kukupatsani zabwino. Matupi anu ndidzaŵalimbitsa. Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri, ngati kasupe wa madzi amene saaphwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:1-2

Tsono abale, popeza kuti Mulungu watichitira chifundo chachikulu chotere, ndikukupemphani kuti mupereke matupi anu omwe kuti akhale nsembe yamoyo, yopatulika, ndi yokondwetsa Mulungu. Imeneyi ikhale njira yanu yopembedzera Mulungu mwauzimu.

Muzikondana kwenikweni monga abale, ndipo muzichita ngati kupikisana poonetsana ulemu.

Potumikira Ambuye, changu chanu chisazilale, koma chikhalebe choyaka.

Muzikhala okondwa chifukwa cha chiyembekezo chanu. Muzipirira pakati pa masautso, ndipo muzipemphera nthaŵi zonse.

Muzipereka zothandiza akhristu anzanu osoŵa, ndipo muziyesetsa kulandira alendo mokondwa.

Pemphani Mulungu kuti aŵadalitse amene amakuzunzani. Ndithu, pemphani kuti aŵadalitse, osaŵatemberera ai.

Muzikondwa nawo amene akukondwa, muzilira nawo amene akulira.

Muzimvana bwino, ndipo musamadzikweze, koma muziyanjana nawo anthu wamba. Musamadziyese anzeru.

Munthu akakuchitani choipa, musamubwezere choipa. Yesani kuchita zimene anthu onse amaziwona kuti nzabwino.

Ngati nkotheka, khalani ndi mtendere ndi anthu onse, monga momwe mungathere.

Okondedwa anga, musabwezere choipa, koma alekeni, mkwiyo wa Mulungu ndiwo uŵalange. Paja Malembo akuti, “Kulipsira nkwanga. Ndidzaŵalanga ndine, akutero Chauta.”

Musamatsanzira makhalidwe a anthu odalira zapansipano, koma Mulungu asinthe moyo wanu wonse pakukupatsani mitima yatsopano. Pamenepo mudzatha kudziŵa zimene Mulungu afuna, ndipo mudzazindikira zimene zili zabwino, zangwiro ndi zomkondwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 42:1-2

Monga momwe mbaŵala imakhumbira mtsinje wamadzi, ndimo m'mene mtima wanga umakhumbira Inu Mulungu wanga.

Kunyoza kwa adani anga kumandipweteka ngati bala lofa nalo la m'thupi mwanga, akamandifunsa nthaŵi zonse kuti, “Mulungu wako ali kuti?”

Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika choncho m'kati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamtamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

Mtima wanga ukumva ludzu lofuna Mulungu, Mulungu wamoyo. Kodi ndidzafika liti pamaso pa Mulungu?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:14

Kuyenda m'njira ya malamulo anu kumandikondwetsa, kupambana kukhala ndi chuma chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 11:5

Pokhala ndi chikhulupiriro, Enoki adatengedwa kupita Kumwamba, osafa konse. Sadapezekenso, popeza kuti Mulungu adamtenga. Malembo amamchitira umboni kuti asanatengedwe, anali wokondweretsa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 4:8

Kuzoloŵeza thupi kumapindulitsapo pang'ono, koma moyo wolemekeza Mulungu umapindulitsa pa zonse. Umatilonjeza moyo pa moyo uno ndiponso pa moyo wakutsogolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 112:1-3

Tamandani Chauta! Ngwodala munthu woopa Chauta, wokonda kusunga malamulo ake.

Munthu woipa amaona zimenezi, ndipo amapsa nazo mtima. Amakukuta mano nazimirira. Zokhumba za munthu woipa sizidzachitika konse.

Zidzukulu zake zidzakhala zamphamvu pa dziko lapansi. Ana a munthuyo adzakhala odala.

Banja lake lidzakhala lachuma ndi lolemera, ndipo kulungama kwake kudzakhala kwamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:8

Potsiriza, abale, muziika mtima pa zilizonse zabwino kwambiri ndi zotamandika, monga izi: zinthu zoona ndi zolemekezeka, zinthu zolungama, zoyera, zokongola, ndi zaulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:28

Njira ya chilungamo imafikitsa ku moyo, koma njira ya zoipa imafikitsa ku imfa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 146:5-6

Ngwodala munthu amene chithandizo chake chimafumira kwa Mulungu wa Yakobe, munthu amene amakhulupirira Chauta, Mulungu wake.

Chauta adalenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili m'menemo. Amasunga malonjezo ake nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 30:19-20

Tsopano ndikukupatsani mpata woti musankhe, kapena moyo kapena imfa, madalitso a Mulungu kapena matemberero ake. Zonse zakumwamba ndi zapansi zikhale mboni za zimene ndakuuzani lerozi. Tsono sankhani moyo,

Tsono inuyo ndi zidzukulu zanu mudzabwerera kwa Chauta, ndipo mau ake amene ndikukupatsani leroŵa mudzaŵamvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.

mukonde Chauta, Mulungu wanu, muzimvera mau ake ndi kukhala okhulupirika kwa Iye, kuti inu ndi zidzukulu zanu mudzakhalitsemo m'dziko limene adalonjeza kuti adzapatsa makolo anu, Abrahamu, Isaki ndi Yakobe.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:9

Tisatope nkuchita zabwino, chifukwa pa nthaŵi yake tidzakolola, ngati sitilefuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:15

Imfa ya anthu oyera mtima a Chauta, ndi yamtengowapatali pamaso pake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 90:12

Tsono tiphunzitseni kuŵerenga masiku athu, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 31:25

Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake. Amaganiza zakutsogolo mosangalala.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:19

Atamandike Ambuye, Mulungu Mpulumutsi wathu, amene amanyamula katundu wathu tsiku ndi tsiku.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 55:22

Tula kwa Chauta nkhaŵa zako, ndipo Iye adzakuchirikiza. Sadzalola konse kuti wolungama wake agwedezeke.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 42:16-17

Pambuyo pake Yobe adakhala ndi moyo zaka 140. Tsono adaona ana ake ndi zidzukulu zake mpaka mbadwo wachinai.

Potsiriza Yobe adamwalira, ali nkhalamba ya masiku ochuluka zedi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 115:14-15

Chauta akudalitseni inu, pamodzi ndi zidzukulu zanu zomwe.

Akudalitseni Chauta, amene adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 10:12-13

Choncho palibe kusiyana pakati pa Ayuda ndi anthu a mitundu ina, pakuti Mulungu ndiye Ambuye a onse, ndipo amadalitsa mooloŵa manja onse otama dzina lake mopemba.

Ndi monga momwe mau a Mulungu anenera kuti, “Aliyense amene adzatama dzina la Ambuye mopemba adzapulumuka.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:21

Zimene umanena zingathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo, munthu wolankhulalankhula adzapeza bwino kapena tsoka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 128:4

Zoonadi, ndimo m'mene adzakhalire wodala munthu woopa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 12:1

Uzikumbukanso Mlengi wako pa masiku a unyamata wako, masiku oipa asanafike, zisanafikenso zaka zoti uzidzati, “Moyowu wandikola.”

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 24:1

Tsopano Abrahamu anali atakalamba, atagonera zaka zochuluka, ndipo Mulungu adaamudalitsa pa zonse zimene ankachita.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 71:9

Musanditaye nthaŵi ya ukalamba wanga, musandisiye ndekha pamene mphamvu zanga zatha,

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:29-31

Amalimbitsa ofooka, ndipo otopa amaŵaonjezera mphamvu.

Kukumveka mau akuti, “Konzani njira ya Chauta m'thengo, lungamitsani mseu wa Mulungu wathu m'chipululu.

Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufooka, ngakhale anyamata amaphunthwa ndi kugwa.

Koma amene amakhulupirira Chauta adzalandira mphamvu zatsopano, adzauluka ngati ziwombankhanga. Adzathamanga koma osatopa, adzayenda koma osalefuka konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:117

Chirikizeni kuti ndipulumuke, kuti nthaŵi zonse ndizitsata malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:16

Ndi nzeru imene imakupatsa moyo wautali. Ndi nzeru imene imakuninkha chuma ndi ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 61:3

Wandituma kuti ndiŵakonzere zofunika olira a ku Ziyoni, ndiye kuti ndiŵapatse maluŵa achisangalalo m'malo mwa phulusa lachisoni, ndiŵapatse mafuta osonyeza kukondwa m'malo mwa kulira, ndiŵapatse chovala cha chikondwerero m'malo mwa kutaya mtima. Tsono adzatchedwa mitengo yamphamvu yachilungamo, yoibzala Chauta, kuti Iye mwini apezepo ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:1-3

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasoŵa kanthu.

Amandigoneka pa busa lamsipu. Amanditsogolera ku madzi odikha kokapumulirako.

Amatsitsimutsa moyo wanga. Amanditsogolera m'njira za chilungamo malinga ndi ulemerero wa dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 29:28

Tsono adamwalira atafika pokalamba zedi. Masiku ake adachuluka, pamodzi ndi chuma ndi ulemerero wake. Ndipo Solomoni, mwana wake, adaloŵa ufumu m'malo mwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 36:5

Inu Chauta, chikondi chanu chosasinthika chimafika mpaka kumwamba, kukhulupirika kwanu kumafika mpaka ku mitambo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:21

Amene amatsata chilungamo ndi chifundo adzapeza moyo ndi ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 65:22

Sadzamanga nyumbazo kuti anthu ena azikhalamo, ndipo sadzabzala mipesayo kuti anthu ena azidyerera zipatso zake. Anthu anga adzakhala ndi moyo wautali ngati mitengo. Ndipo anthu anga osankhidwa adzakondwerera ntchito za manja ao nthaŵi yaitali.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 3:1-2

Pansi pano chinthu chilichonse chili ndi nyengo yake ndi nthaŵi yake yomwe adaika Mulungu:

Ndaziwona ntchito zimene Mulungu adapatsa anthu kuti azizigwira.

Adapanga chinthu chilichonse kuti chikhale chabwino pa nthaŵi yake. M'mitima mwa anthu Mulungu adaikanso nzeru zotanthauzira zochitika za pa mibadwo ndi mibadwo. Komabe anthuwo sangathe kuzitulukira ntchito zonse za Mulungu kuyambira pa chiyambi mpaka pomalizira.

Ndikudziŵa kuti kwa anthu palibe chabwino china choposa kukhala osangalala ndi kumadzikondweretsa nthaŵi yonse ya moyo wao.

Ndi mphatso ya Mulungu kwa anthu kuti azidya, azimwa ndi kumakondwera ntchito zao zolemetsa.

Ndikudziŵa kuti zimene Mulungu amazichita zimakhazikika mpaka muyaya. Palibe zimene zingathe kuwonjezedwa kapena kuchotsedwapo pa zimenezo. Mulungu adazipanga motero, kuti choncho anthu azimumvera.

Zimene zilipo tsopano zidaaliponso kale. Zimene zidzakhalepo kutsogolo, zidaaliponso kale. Mulungu amabwezanso zakale zimene zidapita kuti zichitikenso.

China chimene ndidachiwona pansi pano ndi ichi: Koyenera kukhala chiweruzo chabwino, komwekonso kumapezeka kuipa mtima. Koyenera kukhala chilungamo, komwekonso kumapezeka zoipa.

Ndiye ine ndidayamba kulingalira kuti, “Mulungu adzaŵaweruza onse, abwino ndi oipa omwe, pakuti adaika nthaŵi yochitikira chinthu chilichonse ndiponso ntchito iliyonse.”

Kunena za anthu, ndinkalingaliranso kuti, “Mulungu amaŵayesa ndi cholinga choti aŵaonetse kuti iwowo sasiyana konse ndi nyama.

Zimene zimachitikira anthu, zomwezonso zimachitikira nyama. Monga chinacho chimafa, chinacho chimafanso. Zonsezo zimapuma mpweya umodzimodzi, munthu saposa nyama. Zonsezi nzopandapake.

pali nthaŵi yobadwa ndi nthaŵi yomwalira, pali nthaŵi yobzala ndi nthaŵi yozula zobzalazo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 100:5

Paja Iye ndi wabwino. Chikondi chake nchamuyaya, kukhulupirika kwake nkosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:22

Madalitso a Chauta ndiwo amalemeretsa, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:22-23

Koma zipatso zimene Mzimu Woyera amabweretsa m'moyo wa munthu ndi izi: Chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, kukhulupirika,

kufatsa ndiponso kudziletsa. Zimenezi palibe lamulo loziletsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:12

Kodi pali munthu woopa Chauta? Munthuyo Chauta adzamphunzitsa njira yoti aitsate.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 15:57

Koma tiyamike Mulungu amene amatipambanitsa mwa Ambuye athu Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:24

Ogwira ntchito mwakhama adzakhala olamulira, koma aulesi adzakhala akapolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 41:10

Usachite mantha chifukwa Ine ndili nawe, usataye mtima, poti Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu, ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:6

Sindikayika konse kuti Mulungu, amene adayamba kuchita ntchito yabwinoyi mwa inu, adzaipitiriza mpaka itatsirizika pa Tsiku la Kubweranso kwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:14

Ndikukutamandani, Inu oopsa ndi odabwitsa. Ntchito zanu zonse nzodabwitsa. Mumandidziŵa bwino kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:28

Ndipo tikudziŵa kuti Mulungu amayendetsa zinthu mwa njira yoti zonse ziŵakomere anthu omukonda ndipo apindulepo. Anthuwo ndi amene Iye amaŵaitana monga momwe Iye adazikonzera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:1-5

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga, moyo wanga wonse umuyamike potchula dzina lake loyera.

Satilanga moyenerera machimo athu, satibwezera molingana ndi zolakwa zathu.

Monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, ndi momwenso chidakulira chikondi chake chosasinthika kwa anthu oopa Chauta.

Monga kuvuma kuli kutali ndi kuzambwe, ndi momwenso amachotsera zolakwa zathu kuti zikhale kutali ndi ife.

Monga bambo amachitira chifundo ana ake, ndi momwenso Chauta amaŵachitira chifundo omulemekeza.

Amadziŵa m'mene adatipangira, amakumbukira kuti ife ndife fumbi.

Kunena za munthu, masiku ake sakhalitsa, ali ngati a udzu, munthuyo amakondwa ngati duŵa lakuthengo.

Koma mphepo ikaombapo, duŵalo pamakhala palibe, siliwonekanso pa malo ake.

Koma chikondi cha Chauta nchamuyaya kwa anthu omumvera, zidzukulu zao zonse amazichitira zolungama.

Anthuwo ndi amene amasunga chipangano chake, amene amakumbukira kusunga malamulo ake.

Chauta wakhazikitsa mpando wake wachifumu kumwamba, ndipo amalamulira zonse mu ufumu wake.

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga, ndipo usaiŵale zabwino zake zonse.

Tamandani Chauta, inu angelo ake, inu amphamvu amene mumamva mau ake, amene mumachita zimene amalamula.

Tamandani Chauta, inu magulu a ankhondo ake onse, atumiki ake ochita zimene Iye afuna.

Tamandani Chauta, inu zolengedwa zake zonse, ku madera onse a ufumu wake. Nawenso mtima wanga, tamanda Chauta!

Ndiye amene amakhululukira machimo ako onse, ndi kuchiritsa matenda ako onse.

Ndiye amene amapulumutsa moyo wako ku manda. Amakuveka chikondi chake chosasinthika ndiponso chifundo chake ngati chisoti chaufumu.

Ndiye amene amakupatsa zabwino nthaŵi zonse za moyo wako, choncho umakhalabe wa mphamvu zatsopano ngati mphungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 42:11

Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika choncho m'kati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamtamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:33

Koma inu, yambani mwafunafuna ufumu wa Mulungu ndi kumachita zimene Iye akufuna, ndipo zina zonsezi adzakupatsaninso.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:4

Kondwa mwa Chauta, ndipo adzakupatsa zimene mtima wako ukukhumba.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:18

Ine ndikutsimikiza kuti masautso amene tikuŵamva tsopano salingana mpang'ono pomwe ndi ulemerero umene Mulungu adakonza kuti adzatiwonetse m'tsogolo muno.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:175

Lolani kuti ndikhale moyo, kuti ndizikutamandani, ndipo malangizo anu azindithandiza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:1-2

Ngodala amene moyo wao ulibe choŵadzudzulira, amene amayenda motsata malamulo a Chauta.

Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse, musalole kuti ndisiye kumvera malamulo anu.

Ndili ndi nzeru kupambana okalamba, pakuti ndimatsata malamulo anu.

Ndimaletsa miyendo yanga kuti isayende m'njira yoipa iliyonse, kuti choncho ndizisunga mau anu.

Sindisiyana nawo malangizo anu, pakuti Inu mudandiphunzitsa

mau anu ndi otsekemera kwambiri ndikaŵalaŵa. Amatsekemera kuposa uchi m'kamwa mwanga.

Ndimakhala ndi nzeru za kumvetsa chifukwa cha malamulo anu. Nchifukwa chake ndimadana ndi njira iliyonse yonyenga.

mau anu ndiye nyale ya mapazi anga, ndipo amaunikira njira yanga.

Ndalumbirira, ndipo ndatsimikiza kuti ndidzamvera malangizo anu olungama.

Ndazunzika koopsa, Chauta, patseni moyo, molingana ndi mau anu aja.

Chauta, landirani mapemphero anga oyamika, ndipo mundiphunzitse malangizo anu.

Moyo wanga uli m'zoopsa nthaŵi zonse, komabe sindiiŵala malamulo anu.

Ndasunga mau anu mumtima mwanga, kuti ndisakuchimwireni.

Anthu oipa anditchera msampha, komabe sindisokera kuchoka m'njira ya malamulo anu.

Malamulo anu ndiye madalitso anga mpaka muyaya, zoonadi, ndiwo amene amasangalatsa mtima wanga.

Mtima wanga muuphunzitse kuti uzikonda malamulo anu nthaŵi zonse.

Ndimadana nawo anthu apaŵiripaŵiri, koma ndimakonda mau anu.

Inu ndinu malo anga obisalako ndiponso chishango changa, ndimakhulupirira mau anu.

Chokereni inu, anthu ochita zoipanu, kuti ine ndizitsata malamulo a Mulungu wanga.

Chirikizeni molingana ndi malonjezo anu aja, kuti ndizikhala ndi moyo, ndipo anthu asandichititse manyazi, chifukwa ndine wokhulupirika.

Chirikizeni kuti ndipulumuke, kuti nthaŵi zonse ndizitsata malamulo anu.

Inu mumaŵakana anthu onse osamvera malamulo anu, zoonadi, kuchenjera kwao nkopandapake.

Anthu onse oipa a pa dziko lapansi, mumaŵayesa ngati zakudzala, nchifukwa chake ndimakonda malamulo anu.

Mutamandike, Inu Chauta, phunzitseni malamulo lanu.

Thupi langa limanjenjemera chifukwa chokuwopani, ndimachita mantha ndi kuweruza kwanu.

Ndachita zimene zili zolungama ndi zabwino. Musandisiye m'manja mwa ondizunza.

Lonjezani kuti mudzandichitira zabwino mtumiki wanune, musalole anthu osasamala za Mulungu kuti andizunze.

Maso anga atopa chifukwa cha kuyembekeza chipulumutso chanu, chifukwa cha kudikira kuti malonjezo anu olungama aja achitikedi.

Komereni mtima mtumiki wanune, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.

Ndine mtumiki wanu, mundipatse nzeru zomvetsa, kuti ndizidziŵa malamulo anu.

Yakwana nthaŵi yakuti Inu Chauta muchitepo kanthu, popeza kuti anthu aphwanya malamulo anu.

Koma ine ndimasamala malamulo anu kupambana golide, golide wosungunula bwino.

Malamulo anu onse amalungamitsa mayendedwe anga. Ndimadana ndi njira iliyonse yonyenga.

Malamulo anu ndi abwino, nchifukwa chake ndimaŵatsata ndi mtima wanga wonse.

Ndimalalika ndi mau anga malangizo onse a pakamwa panu.

Kufotokozera mau anu kumakhala ngati kuŵala, kumapatsa nzeru za kumvetsa kwa anthu opanda nzeru.

Ndimapuma mwaŵefuŵefu nditatsekula pakamwa, chifukwa ndimalakalaka malamulo anu.

Yang'aneni, ndipo mundikomere mtima monga m'mene mumachitira ndi anthu okukondani.

Chirikizani mayendedwe anga molingana ndi mau anu aja, musalole kuti tchimo lililonse lizindilamulira.

Pulumutseni kwa anthu ondizunza, kuti ndizitsata malamulo anu.

Yang'anireni ine mtumiki wanu ndi chikondi chanu, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.

Maso anga akudza misozi yambiri ngati mitsinje, chifukwa anthu satsata malamulo anu.

Ndinu olungama Chauta, ndipo kuweruza kwanu nkolungama.

Malamulo amene mwatipatsa, ndi olungama ndi okhulupirika ndithu.

Changu changa chikuyaka ngati moto mumtima mwanga, chifukwa adani anga amaiŵala mau anu.

Kuyenda m'njira ya malamulo anu kumandikondwetsa, kupambana kukhala ndi chuma chilichonse.

Malonjezo anu ndi otsimikizika, ndipo ine mtumiki wanu ndimaŵakonda.

Ine ndine wamng'ono ndi wonyozeka, komabe sindiiŵala malamulo anu.

Kulungama kwanu nkwamuyaya, ndipo malamulo anu ndi oona.

Mavuto andigwera pamodzi ndi zoŵaŵa zomwe, koma malamulo anu amandisangalatsa.

Malamulo anu ndi olungama mpaka muyaya, patseni nzeru zomvetsa kuti ndizikhala ndi moyo.

Ndikulira kwa Inu ndi mtima wanga wonse, mundiyankhe, Inu Chauta. Ndidzatsata malamulo anu.

Ndikukulirirani, mundipulumutse, kuti ndizitsata malamulo anu.

Ndimadzuka tambala asanalire, kuti ndipemphe chithandizo. Ndimakhulupirira mau anu.

Ndimakhala maso usiku wonse, ndikusinkhasinkha za malonjezo anu.

Imvani liwu langa chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika. Inu Chauta, sungani moyo wanga chifukwa cha chilungamo chanu.

Ndidzasinkhasinkha za malamulo anu, ndipo ndidzatsata njira zanu.

Anthu ankhanza ondizunza akuyandikira. Iwo ali kutali ndi malamulo anu.

Koma Inu Chauta muli pafupi, ndipo malamulo anu onse ndi oona.

Poŵerenga malamulo anu ndidadziŵa kale lomwe kuti Inu mudaŵakhazikitsa mpaka muyaya.

Yang'anani masautso anga, ndipo mundipulumutse, popeza kuti sindiiŵala malamulo anu.

Munditchinjirize pa mlandu wanga, ndipo mundiwombole. Mundipatse moyo molingana ndi malonjezo anu aja.

Chipulumutso chili kutali ndi anthu oipa, pakuti safunafuna malamulo anu.

Chifundo chanu nchachikulu, Inu Chauta, mundipatse moyo molingana ndi chilungamo chanu.

Anthu ondizunza ndiponso adani anga ngochuluka, koma sindisiyana nawo malamulo anu.

Ndimanyansidwa ndikamayang'ana anthu osakhulupirika, chifukwa satsata malamulo anu.

Onani m'mene ndimakondera malamulo anu, sungani moyo wanga chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika

Ndidzakondwera ndi malamulo anu, ndipo mau anu sindidzaŵaiŵala.

mau anu ndi oona okhaokha, malangizo anu onse olungama ngamuyaya.

Mafumu amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umaopa mau anu.

Ndimakondwa ndi mau anu monga munthu amene wapeza chuma chambiri.

Ndimadana ndi anthu abodza, zoonadi, ndimanyansidwa nawo, koma ndimakonda malamulo anu.

Ndimakutamandani kasanunkaŵiri pa tsiku, chifukwa cha malangizo anu olungama.

Anthu okonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, palibe china chotha kuŵagwetsa.

Ndimakhulupirira kuti mudzandipulumutsa, Inu Chauta, ndipo ndimatsata malamulo anu.

Mzimu wanga umatsata malamulo anu, pakuti ndimaŵakonda ndi mtima wanga wonse.

Ndimatsata malamulo anu ndi malangizo anu, pakuti makhalidwe anga onse mukuŵaona.

Kulira kwanga kumveke kwa Inu, Chauta. Mundipatse nzeru zomvetsa potsata mau anu aja.

Komereni mtima ine mtumiki wanu, kuti ndikhale ndi moyo ndi kusunga mau anu.

Kupempha kwanga kumveke kwa Inu. Mundipulumutse potsata malonjezo anu.

Pakamwa panga padzakutamandani, chifukwa mumandiphunzitsa malamulo anu.

Ndidzaimba nyimbo zoyamikira mau anu, chifukwa malamulo anu onse ndi olungama.

Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza, chifukwa ndatsata malamulo anu.

Ndikulakalaka nthaŵi yoti mudzandipulumutse. Inu Chauta, malamulo anu amandikondwetsa.

Lolani kuti ndikhale moyo, kuti ndizikutamandani, ndipo malangizo anu azindithandiza.

Ndasokera ngati nkhosa yoloŵerera, koma mundifunefune ine mtumiki wanu, pakuti sindiiŵala malamulo anu. Nyimbo yoimba pokwera ku Yerusalemu.

Tsekulani maso anga kuti ndiwone zodabwitsa zochokera m'malamulo anu.

Ndine munthu wongokhala nawo pa dziko lapansi, musandibisire malamulo anu.

Ngodala amene amasunga malamulo a Chauta, amene amafunafuna Chauta ndi mtima wao wonse,

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 7:1

Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino amtengowapatali. Tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 56:3-4

Pamene ndichita mantha ndimadalira Inu.

Ndimatamanda Mulungu chifukwa cha zimene wandilonjeza. Ndimakhulupirira Mulungu mopanda mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:105

mau anu ndiye nyale ya mapazi anga, ndipo amaunikira njira yanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:7

Musadzinyenge, nkosatheka kupusitsa Mulungu. Zimene munthu amabzala, adzakolola zomwezo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:14

Chauta amapalana chibwenzi ndi anthu omvera Iye, ndipo amaŵadziŵitsa chipangano chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:11

Pakuti Chauta ndiye dzuŵa ndi chishango, amatichitira chifundo ndi kutipatsa ulemu. Chauta saŵamana zabwino anthu oyenda molungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 20:12

“Uzilemekeza atate ndi amai ako, kuti masiku a moyo wako achuluke m'dziko limene Chauta, Mulungu wako, akukupatsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:12-14

Ndani mwa inu amakhumba moyo ndi kulakalaka kuti akhale masiku ambiri, kuti asangalale ndi zinthu zabwino?

Ngati ufunadi moyo, usalankhule zoipa, pakamwa pako pasakambe zonyenga.

Lewa zoipa, ndipo uchite zabwino. Funafuna mtendere ndi kuulondola.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:10

Mwana wanga, umvere ndi kuvomera zimene ndikunena. Ukatero, zaka za moyo wako zidzachuluka.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 22:4

Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Chauta, ndi chuma, ulemu ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:15-16

Akadzandiitana, ndidzamuyankha, ndidzakhala naye pa nthaŵi yamavuto. Ndidzamlanditsa ndi kumlemekeza.

Ndidzampatsa moyo wautali ndi kumpulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:2-3

Mau a Mulungu akuti, “Lemekeza atate ako ndi amai ako.” Limeneli ndiye lamulo loyamba kukhala ndi lonjezo.

Ngakhale ndili womangidwa m'ndende, ndine nthumwi ndithu chifukwa cha Uthenga Wabwinowu. Mundipempherere tsono kuti ndizilankhula molimba mtima za Uthenga Wabwinowu, monga ndiyenera kulankhulira.

Tikiko adzakudziŵitsani zonse za ine ndi zimene ndikuchita. Iyeyu ndi mbale wathu wokondedwa, ndiponso mtumiki wokhulupirika pa ntchito ya Ambuye.

Ndikumtuma kwa inu kuti mudziŵe za m'mene tiliri, ndipo kuti akulimbitseni mtima.

Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu apatse abale onse mtendere, chikondi ndi chikhulupiriro.

Onse okonda Ambuye athu Yesu Khristu ndi chikondi chosafa, Mulungu aŵadalitse.

Lonjezolo likuti, “Ukatero, udzakhala wodala, ndipo moyo wako udzakhala wautali pansi pano.”

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wachikondi, zikomo kwambiri pa moyo umene mwandipatsa. Ndikudziwa kuti mpaka pano mwanditeteza ndi kundisunga ku zoopsa zambiri, mwandikomera mtima ndi kundisonyeza chikondi chanu chachikulu. Ndikupemphani Ambuye, mundithandize kukhala moyo wanga wonse ndikukulemekezani ndi kutsatira mawu anu monga momwe mumakondera. Munditeteze ku mtima wosamvera ndi wodzikuza chifukwa ndikufuna kukhala ndi moyo wautali, koma ndikudziwa kuti malonjezano anu amakwaniritsidwa pokhapokha ndikamvera mawu anu ndi kuyenda monga momwe mukufunira. Mawu anu amati: "Mverani mwananga, landirani mawu anga, ndipo zaka zanu za moyo zidzachuluka." Mundikhululukire ngati ndakhala wosamvera, ngati ndachita zomwe mtima wanga ukufuna m'malo modzitsogolera ndi Mzimu wanu Woyera. Ndi mtima wanga wonse, ndikufuna kukhala ndi khutu lomvera mawu ndi malamulo anu, komanso kukhala kutali ndi zoyipa zonse. Mundipatse mtima woyera kuti ndikukondweretseni masiku onse a moyo wanga. M'dzina la Yesu. Ameni.