Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

146 Mau a Mulungu: Chikumbutso Chakuti Iye Ndi Thanthwe Lathu


Masalimo 18:2

Chauta ndiye thanthwe langa, linga langa ndi mpulumutsi wanga. Ndiye Mulungu wanga, ndi thanthwe langa limene ndimathaŵirako. Ndiye chishango changa, ndiye mtetezi wanga ndi mpulumutsi wanga, ndiye linga langa.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 22:2-3

Davideyo adaimbira Chauta nyimbo iyi yakuti, “Chauta ndiye thanthwe langa, linga langa ndi mpulumutsi wanga.

Adakandifikitsa ku malo amtendere, adandipulumutsa chifukwa adakondwera nane.

“Chauta adandipatsa mphotho molingana ndi kulungama kwanga, adandifupa molingana ndi ungwiro wanga.

Ine ndidatsata njira za Chauta sindidachite zoipa ndi kumsiya Mulungu wanga.

Ndidamvera malangizo ake onse, ndipo malamulo ake sindidaŵataye.

Ndinalibe mlandu pamaso pake, ndinkalewa zoipa m'moyo wanga.

Nchifukwa chake Chauta wandipatsa mphotho molingana ndi kulungama kwanga, monga momwe akuwonera kuti ndilibe mlandu.

“Kwa anthu okhulupirika, Inu Mulungu mumadziwonetsa okhulupirika, kwa anthu aungwiro mumadziwonetsa abwino kotheratu.

Kwa anthu oyera mtima mumadziwonetsa okoma mtima, koma kwa anthu oipa mtima mumadziwonetsa ochenjera koposa.

Paja anthu odzichepetsa Inu mumaŵapulumutsa, koma anthu odzikuza mumaŵatsitsa.

Ndithu Inu Chauta, ndinu nyale yanga, Inu Mulungu, mumandiwunikira mu mdima.

Ndiye Mulungu wanga ndi thanthwe langa limene ndimathaŵirako. Ndiye chishango changa, ndiye mtetezi wanga ndi mpulumutsi wanga. Ndiye linga langa ndi mpulumutsi wanga. Ndinu amene mumandiwombola pa nkhondo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 62:2

Iye yekhayo ndiye thanthwe langa, chipulumutso changa, ndi linga langa. Sindidzagwedezeka konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 62:6-7

Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa, ndiye linga langa ndipo sindidzagwedezeka.

Chipulumutso changa ndi ulemerero wanga, zonsezo zili kwa Mulungu. Mulungu ndiye thanthwe langa lamphamvu, ndiye kothaŵira kwanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 26:4

Inu anthu, mukhulupirire Chauta mpaka muyaya, chifukwa chakuti Chauta Mulungu ndiye thanthwe losatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 94:22

Koma Chauta wasanduka linga langa londiteteza, Mulungu ndiye thanthwe langa lothaŵirako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:3

Zoonadi, ndinu thanthwe langa ndi linga langa. Tsogolereni ndi kundiwongolera chifukwa Inu ndinu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 144:1

Atamandike Chauta, thanthwe langa londitchinjiriza, amene amaphunzitsa manja anga ndi zala zanga kumenya nkhondo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 10:4

Onse ankamwanso chakumwa chauzimu chimodzimodzi, pakuti analikumwa m'thanthwe lauzimu limene linkaŵatsatira. Thanthwelo linali Khristu yemwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 32:4

Chauta ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama, ndi Mulungu wokhulupirika ndi wosaipa konse, wachilungamo ndi wosalakwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 18:31

Palibe mulungu wina koma Chauta yekha. Palibe thanthwe lina lothaŵirapo koma Mulungu wathu yekha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 28:1

Ndikuitana Inu Chauta, Inu thanthwe langa, musachite ngati simukundimva, chifukwa ngati mukhala chete, ndidzafanafana ndi anthu otsikira ku manda.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 22:47

“Chauta ndiwamoyo. Litamandike thanthwe langa, alemekezeke Mulungu wanga, thanthwe londipulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 89:26

“Iye adzandiwuza kuti, ‘Inu ndinu Atate anga, Mulungu wanga, Thanthwe londipulumutsa.’

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 71:3

Mundikhalire thanthwe lothaŵirako, ndiponso linga lolimba lopulumukirako. Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 61:2

Ine wokhala ku mathero a dziko lapansi, ndataya mtima, ndipo ndikuitana Inu. Munditsogolere ku thanthwe lalitali.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 44:8

Musadedere, musaope. Suja kuyambira kale lomwe ndakhala ndikukuuzani ndi kutsimikiza zimenezi? Inuyo ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Iyai, palibenso Thanthwe lina, sindikudziŵa lina lililonse.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 92:15

imaonetsa kuti Chauta ndi wolungama. Iye ndiye thanthwe langa mwa Iye mulibe chokhota.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 46:1-2

Mulungu ndiye kothaŵira kwathu, ndiye mphamvu zathu. Ali wokonzekeratu kutithandiza pa nthaŵi yamavuto.

“Khalani chete, ndipo mudziŵe kuti ndine Mulungu. Mitundu ya anthu imanditamanda, a m'dziko lapansi amandiyamika.”

Chauta Wamphamvuzonse ali nafe, Mulungu wa Yakobe ndiye kothaŵira kwathu.

Nchifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisinthike, ngakhale mapiri agwe pakati pa nyanja zozama,

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 32:18

Adakana mtetezi wao amene adaŵalenga, adaiŵala Mulungu amene adaŵapatsa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 17:10

Inu Aisraele, mwaiŵala Mulungu Mpulumutsi wanu, simudamkumbukire Iye amene ndiye thanthwe lokupulumutsani. M'malo mwake, mumabzala mbeu zabwino, kubzalira milungu yachilendo,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 62:1-2

Mtima wanga umakhala chete kuyembekezera Mulungu yekha, pakuti chipulumutso changa chimafumira kwa Iye.

Musakhulupirire kuti zachiwawa zingakuthandizeni. Musaganize kuti kuba kungakupindulitseni. Chuma chikachuluka musaikepo mtima.

Mulungu adalankhula kamodzi, ine ndaphunzirapo zinthu ziŵiri, china ndi chakuti mphamvu ndi zanu, Inu Mulungu,

chikondi chanu nchosasinthika, Inu Ambuye; china ndi chakuti Inu mumabwezera munthu molingana ndi ntchito zake.

Iye yekhayo ndiye thanthwe langa, chipulumutso changa, ndi linga langa. Sindidzagwedezeka konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 42:9

Ndimafunsa Mulungu, thanthwe langa, kuti, “Mwandiiŵaliranji? Ndiziyenderanji ndilikulira chifukwa chondipsinja mdani wanga?”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:2-3

Tcherani khutu kuti mundimve, fulumirani kudzandipulumutsa. Mukhale thanthwe langa lothaŵirako, ndi linga langa lolimba londipulumutsa.

Mumaŵabisa pamalo pamene pali Inu, kuti muŵateteze ku ziwembu za adani ao. Mumaŵasunga bwino ndi kuŵatchinjiriza, kuti anthu angakangane nawo.

Atamandike Chauta: wandiwonetsa modabwitsa chikondi chake chosasinthika, pamene ndinali mu mzinda wozingidwa ndi gulu la ankhondo.

Ndidalankhula mwankhaŵa kuti, “Andipirikitsira kutali ndi Inu.” Koma Inu mudamva kupempha kwanga pamene ndidakudandaulirani kuti mundithandize.

Kondani Chauta, inu nonse anthu oyera mtima. Chauta amasunga anthu okhulupirika, koma amalanga koopsa anthu odzikuza.

Khalani amphamvu ndipo mulimbe mtima, inu nonse okhulupirira Chauta.

Zoonadi, ndinu thanthwe langa ndi linga langa. Tsogolereni ndi kundiwongolera chifukwa Inu ndinu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 33:21-22

Adapitirira kunenanso kuti, “Pafupi ndi Ine pano pali thanthwe, iwe uimirire pathanthwepo.

Tsono ulemerero wanga ukamapita, ndikuika mu mng'alu wa thanthwe, ndipo ndikuphimba ndi dzanja langa mpaka nditabzola.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 73:26

Thupi langa ndi mtima wanga zingafooke chotani, Mulungu ndiye mphamvu za mtima wanga ndiyenso wondigaŵira madalitso mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 30:29

Koma inu anthu a Mulungu, mudzakondwa ndi kuimba monga m'mene mumachitira usiku pa chikondwerero chopatulika. Mudzasangalala ngati anthu opita naimba toliro ku phiri la Chauta, thanthwe la Israele.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 27:5

Pa tsiku lamavuto adzandibisa ndi kunditchinjiriza. Adzandisunga m'kati mwa Nyumba yake, adzanditeteza pa thanthwe lalitali.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:1-2

Munthu amene amakhala m'linga la Wopambanazonse, iye amene amakhala mumthunzi mwa Mphambe,

zoipa sizidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi nyumba yako.

Chauta adzapatsa angelo ake ntchito yoti azikulonda kulikonse kumene upite.

Adzakunyamula m'manja mwao, kuwopa kuti phazi lako lingapweteke ndi mwala.

Udzatha kuponda mkango ndi njoka, zoonadi udzaponda ndi phazi lako msona wa mkango ndiponso chinjoka.

Pakuti amene amandikangamira Ine Mulungu mwachikondi, ndidzampulumutsa. Ndidzamteteza popeza kuti amadziŵa dzina langa.

Akadzandiitana, ndidzamuyankha, ndidzakhala naye pa nthaŵi yamavuto. Ndidzamlanditsa ndi kumlemekeza.

Ndidzampatsa moyo wautali ndi kumpulumutsa.

adzanena kwa Chauta kuti, “Inu ndinu kothaŵira kwanga ndi linga langa, ndinu Mulungu wanga amene ndimakukhulupirirani.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 32:2

Aliyense mwa iwo adzakhala ngati pothaŵirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe. Adzakhala ngati mitsinje yoyenda m'dziko louma, ndipo ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu m'chipululu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:24-25

“Munthu aliyense womva mau angaŵa nkumaŵagwiritsa ntchito, amafanafana ndi munthu wanzeru amene adaamanga nyumba yake pa thanthwe.

Kudagwa mvula, mitsinje idadzaza, ndipo chimphepo chidadza nkuwomba pa nyumbayo. Koma siidagwe, chifukwa chakuti adaaimanga polimba.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 32:31

Adani ao amadziŵa kuti milungu yao ndi yopanda mphamvu, ndi yosalingana ndi Mulungu wa Aisraele.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 22:32

“Palibe Mulungu wina koma Chauta yekha. Palibe thanthwe lina lothaŵirapo koma Mulungu wathu yekha?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 27:1

Chauta ndiye muuni wanga ndi chipulumutso changa. Ndidzaopa yani? Chauta ndiye linga la moyo wanga, nanga ndichitirenji mantha?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:24

Khalani amphamvu ndipo mulimbe mtima, inu nonse okhulupirira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 51:1

Chauta akunena kuti: “Tcherani khutu inu amene mufuna kupulumuka, inu amene mufuna kuti ndikuthandizeni. Taganizani za thanthwe kumene mudasemedwa, ku nkhuti ya miyala kumene adakukumbani.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 62:8

Anthu inu, ikani mtima wanu pa Iye nthaŵi zonse. Muuzeni zonse za kukhosi kwanu. Mulungu ndiye kothaŵira kwathu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 94:18

Pamene ndinkaganiza kuti, “Phazi langa likuterereka,” nkuti chikondi chanu chosasinthika chikundichirikiza.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 22:3

Ndiye Mulungu wanga ndi thanthwe langa limene ndimathaŵirako. Ndiye chishango changa, ndiye mtetezi wanga ndi mpulumutsi wanga. Ndiye linga langa ndi mpulumutsi wanga. Ndinu amene mumandiwombola pa nkhondo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:22

Mwala umene amisiri omanga nyumba adaukana, womwewo wasanduka mwala wapangodya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 18:46

Chauta ndi wamoyo. Litamandike thanthwe langa, alemekezeke Mulungu wondipulumutsa,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:4-5

Bwerani kwa Iye amene ali mwala wamoyo womwe anthu adaukana, koma Mulungu adausankha kuti ngwamtengowapatali.

Inunso mukhale ngati miyala yamoyo yoti Mulungu amangire nyumba yake. M'menemo muzitumikira ngati ansembe opatulika, pakupereka nsembe zochokera ku mtima, zokomera Mulungu kudzera mwa Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 71:1-2

Ine ndimathaŵira kwa Inu Chauta. Musandichititse manyazi.

Adani anga amandinena, anthu olondalonda moyo wanga amapangana limodzi,

namanena kuti, “Mulungu wamsiya yekha. Mlondoleni, mumgwire, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe woti ampulumutse.”

Inu Mulungu, musandikhalire kutali. Inu Mulungu wanga, fulumirani kudzandithandiza.

Anthu ondineneza achite manyazi ndipo aonongeke. Anthu ofunafuna kundipweteka anyozedwe, ndipo achite manyazi kotheratu.

Koma ine ndidzakhulupirira Inu nthaŵi zonse, ndipo ndidzapitirizabe kukutamandani.

Pakamwa panga padzalankhula tsiku lonse za ntchito zanu zolungama ndi za chipulumutso chanu, popeza kuti sindidziŵa chiŵerengero chake.

Ndidzabwera ndi uthenga wofotokoza za ntchito zamphamvu za Chauta. Ndidzatamanda chilungamo chanu chokha.

Inu Mulungu, mwandiphunzitsa kuyambira ubwana wanga, ndipo ndikulalikabe ntchito zanu zodabwitsa.

Choncho Inu Mulungu, musandisiye ndekha ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbu, mpaka nditalalika mphamvu zanu kwa mibadwo yonse yakutsogolo.

Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu, zimafikira mpaka kumwambamwamba. Pali yani wofanafana nanu, Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?

Koma mundilanditse ndi kundipulumutsa, pakuti ndinu Mulungu wolungama. Tcherani khutu kuti mundimve, ndipo mundipulumutse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:10

Chauta ali ngati nsanja yolimba, munthu wokhulupirira amathaŵiramo napulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 16:8

Nthaŵi zonse ndimalingalira za Chauta. Popeza kuti ali ku dzanja langa lamanja, palibe amene angandiopse konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 27:14

Tsono khulupirira Chauta. Khala wamphamvu, ndipo ulimbe mtima. Ndithu, khulupirira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 9:9

Kwa Chauta ndiye kothaŵirako anthu opsinjidwa, ndiyenso kopulumukira pa nthaŵi yamavuto.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:9

Chifukwa chakuti wavomera Chauta kuti akhale malo ako othaŵirako, wavomera Wopambanazonse kuti akhale malo ako okhalamo,

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 32:37

Pamenepo Chauta adzafunsa anthu ake kuti, “Nanga milungu yamphamvu yomwe mumaikhulupirira ija ili kuti?

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 28:16

Tsopano zimene akunena Ambuye Chauta nzakuti, “Ku Ziyoni ndikuika maziko a mwala wotsimikizika, mwala wapangodya wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu. Pamwalapo palembedwa kuti, ‘Wokhulupirira sadzagwedezeka.’

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 17:7

Onetsani chifundo chanu pakuchita zodabwitsa, Inu amene mumaŵapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja onse obwera kwa Inu, kuthaŵa adani ao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:39-40

Chipulumutso cha anthu abwino chimachokera kwa Chauta. Chauta ndiye kothaŵirako anthuwo pa nthaŵi yamavuto.

Kondwa mwa Chauta, ndipo adzakupatsa zimene mtima wako ukukhumba.

Chauta amaŵathandiza ndi kuŵalanditsa. Amaŵachotsa m'manja mwa anthu oipa nkuŵapulumutsa, popeza kuti anthuwo amadalira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 46:7

Chauta Wamphamvuzonse ali nafe. Mulungu wa Yakobe ndiye kothaŵira kwathu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 2:2

“Palibe woyera wina wofanafana ndi Chauta, palibe wina koma Iye yekha. Palibe thanthwe lina lotchinjiriza lofanafana ndi Mulungu wathu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 22:13

M'kuŵala kumene kunali pamaso pake munkafumira makala amoto alaŵilaŵi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:2

Adanditulutsa m'dzenje la chiwonongeko, m'chithaphwi chamatope. Adapondetsa mapazi anga pa thanthwe, nandiyendetsa bwino lomwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 125:1

Anthu amene amakhulupirira Chauta ndi olimba ngati phiri la Ziyoni, limene silingathe kugwedezeka, koma ndi lokhala mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:18-19

Chauta ali pafupi ndi onse amene amamutama mopemba. Ali pafupi ndi onse amene amamutama mokhulupirika.

Amene amamvera Chauta, amaŵapatsa zofuna zao, amamvanso kulira kwao, naŵapulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 43:2

Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe, pamene ukuwoloka mitsinje, siidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto sudzapsa, malaŵi ake sadzakutentha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 33:6

Adzakupatsani mtendere wokhazikika pa nthaŵi yanu. Adzakuninkhaninso chipulumutso chachikulu, luntha lambiri ndi nzerunso zambiri. Kuwopa Chauta ndiko kumapezetsa chuma chimenechi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:4

Ngakhale ndiyende m'chigwa chamdima wabii, sindidzaopa choipa chilichonse, pakuti Inu Ambuye mumakhala nane. Chibonga chanu ndi ndodo yanu zimanditeteza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 55:22

Tula kwa Chauta nkhaŵa zako, ndipo Iye adzakuchirikiza. Sadzalola konse kuti wolungama wake agwedezeke.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:14

Chauta amene ndimamuimbira ndiye mphamvu zanga. Ndiye mpulumutsi wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 30:5

Mkwiyo wake ndi wa kanthaŵi chabe, koma kukoma mtima kwake nkwa moyo wonse. Misozi ingachezere kugwa usiku, m'maŵa kumabwera chimwemwe chokhachokha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 32:27

“Ine ndine Chauta, Mulungu wa anthu onse. Kodi chilipo choti Ine nkundikanika?

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:13

Ndingathe kuchita zonse chifukwa Khristu amandipatsa mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Atesalonika 3:3

Koma Ambuye ngokhulupirika, ndipo adzakulimbitsani mtima ndi kukutchinjirizani kwa Woipa uja.

Mutu    |  Mabaibulo
Nahumu 1:7

Chauta ndi wabwino, ndiye kothaŵira pa nthaŵi yamavuto. Amasamala onse amene amadalira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:29

Amalimbitsa ofooka, ndipo otopa amaŵaonjezera mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 14:14

Chauta ndiye amene akumenyereni nkhondo. Inuyo simuchitapo kanthu konse.”

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 11:28-30

“Bwerani kwa Ine, inu nonse otopa ndi olemedwa, ndipo Ine ndidzakupatsani mpumulo.

Senzani goli langa ndipo phunzirani kwa Ine, pakuti ndine wofatsa ndi wa mtima wodzichepetsa; mukatero mudzapeza mpumulo m'mitima mwanu.

“Kodi Inu ndinu uja ankati adzabwerayu, kapena tiziyembekezera wina?”

Pajatu goli limene ndimakoleka Ine nlosavuta, ndipo katundu amene ndimasenzetsa Ine ngwopepuka.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 41:10

Usachite mantha chifukwa Ine ndili nawe, usataye mtima, poti Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu, ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:31

Nanga tsono tinganenenso chiyani pa zonsezi? Ngati Mulungu ali pa mbali yathu, angatsutsane nafe ndani?

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 12:2

“Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga, ndidzamkhulupirira Iye, ndipo sindidzaopa. Pakuti Chauta ndiye mphamvu zondilimbitsa, ndiye amene ndimamuimbira, ndiye Mpulumutsi wanga.”

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:6

Tiyeni tsono tilimbe mtima ndi kunena kuti, “Ambuye ndiwo Mthandizi wanga, sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?”

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 14:27

“Ndikukusiyirani mtendere. Ndikukupatsani mtendere wanga. Sindikukupatsani mtenderewo monga m'mene dziko lino lapansi limapatsira ai. Mtima wanu usavutike kapena kuda nkhaŵa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 3:3

Koma Inu Chauta, ndinu chishango changa chonditeteza, ndinu ulemerero wanga, mumalimbitsa mtima wanga ndinu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yoswa 1:9

Paja ndidakulamula kuti ukhale wamphamvu. Usamaopa kapena kutaya mtima, poti Ine, Chauta, Mulungu wako, ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 46:10

“Khalani chete, ndipo mudziŵe kuti ndine Mulungu. Mitundu ya anthu imanditamanda, a m'dziko lapansi amandiyamika.”

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:10

Potsiriza ndikuti, dzilimbitseni mwa Ambuye, mwa mphamvu yao yaikulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:31

Koma amene amakhulupirira Chauta adzalandira mphamvu zatsopano, adzauluka ngati ziwombankhanga. Adzathamanga koma osatopa, adzayenda koma osalefuka konse.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 5:7

Tulani pa Iye nkhaŵa zanu zonse, popeza kuti Iye ndiye amakusamalirani.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 27:3

Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzachita mantha konse. Ngakhale nkhondo ibuke kulimbana nane, ine sindidzaleka kukhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 25:4

Inu mwakhala ngati ngaka kwa anthu osauka, mwakhala ngati linga kwa anthu osoŵa pa nthaŵi yamavuto. Mwakhala ngati pobisalirapo namondwe, ndiponso ngati mthunzi wousirapo dzuŵa. Anthu ankhalwe ali ngati namondwe woomba pa khoma, ngati chitungu m'dziko louma.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 22:19

Adaniwo adandithira nkhondo pamene ndinali m'mavuto, koma Chauta adandichirikiza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 62:11-12

Mulungu adalankhula kamodzi, ine ndaphunzirapo zinthu ziŵiri, china ndi chakuti mphamvu ndi zanu, Inu Mulungu,

chikondi chanu nchosasinthika, Inu Ambuye; china ndi chakuti Inu mumabwezera munthu molingana ndi ntchito zake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 66:2

Imbani nyimbo zoyamika dzina lake laulemerero, mumtamande mwaulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 71:5

Inu Ambuye, ndinu amene ndimakukhulupirirani, Inu Chauta, ndinu amene ndimakudalirani kuyambira ubwana wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 22:1

Tsiku limene Chauta adaapulumutsa Davide kwa adani ake onse ndiponso kwa Saulo,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:11

Muzidalira Chauta ndi mphamvu zake. Muziyesetsa kukhala pamaso pake kosalekeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:6-7

Musade nkhaŵa ndi kanthu kalikonse, koma m'mapemphero anu onse muzipempha Mulungu zimene zikusoŵani, ndipo nthaŵi zonse muzipemphe ndi mtima woyamika.

Pamenepo mtendere wochokera kwa Mulungu, umene uli wopitirira nzeru zonse za anthu, udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:13

Mulungu amene amatipatsa chikhulupiriro, adzaze mitima yanu ndi chimwemwe ndi mtendere pakumvera Iye, kuti chiyembekezo chanu chizikulirakulira ndi mphamvu za Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:14-16

Pakuti amene amandikangamira Ine Mulungu mwachikondi, ndidzampulumutsa. Ndidzamteteza popeza kuti amadziŵa dzina langa.

Akadzandiitana, ndidzamuyankha, ndidzakhala naye pa nthaŵi yamavuto. Ndidzamlanditsa ndi kumlemekeza.

Ndidzampatsa moyo wautali ndi kumpulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:5-6

Uzikhulupirira Chauta ndi mtima wako wonse, usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.

Pa ntchito zako zonse uzivomera kuti kuli Mulungu, choncho njira zako Iye adzazilungamitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:16

Tiyeni tsono, tiyandikire mopanda mantha ku mpando wachifumu wa Mulungu wokoma mtima. Kumeneko tidzalandira chifundo, ndipo mwa kukoma mtima kwa Mulungu tidzapeza thandizo pa nthaŵi yake yeniyeni.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:28

Ndipo tikudziŵa kuti Mulungu amayendetsa zinthu mwa njira yoti zonse ziŵakomere anthu omukonda ndipo apindulepo. Anthuwo ndi amene Iye amaŵaitana monga momwe Iye adazikonzera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 61:3-4

Inutu ndinu kothaŵira kwanga, nsanja yolimba yonditeteza kwa adani.

Mundilole ndizikhala m'Nyumba mwanu nthaŵi zonse. Mundilole ndibisale pansi pa mapiko anu kuti munditeteze.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:4-5

Chifukwa aliyense amene ali mwana wa Mulungu, amagonjetsa dziko lapansi. Chimene timagonjetsera dziko lapansilo ndi chikhulupiriro chathu.

Ndani amagonjetsa dziko lapansi? Amaligonjetsa si wina ai, koma wokhulupirira kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 16:33

Ndakuuzani zimenezi kuti mukhale nawo mtendere pakukhulupirira Ine. M'dziko lapansi mudzaona masautso, koma limbikani, Ine ndagonjetsa mphamvu zoipa za dziko lapansi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:4

Ndidapemphera kwa Chauta ndipo adandiyankha. Adandipulumutsa kwa zonse zimene ndinkaziwopa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:18

Chauta ali pafupi ndi onse amene amamutama mopemba. Ali pafupi ndi onse amene amamutama mokhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 63:7-8

Inu mwakhala chithandizo changa, motero ndikuimba ndi chimwemwe pansi pa mapiko anu.

Mtima wanga ukukangamira Inu, dzanja lanu lamanja likundichirikiza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 89:1-2

Inu Chauta, ndidzaimba mosalekeza nyimbo yotamanda chikondi chanu chosasinthika. Ndidzalalika ndi pakamwa panga za kukhulupirika kwanu ku mibadwo yonse.

Mudatswanya chilombo cha m'nyanja ndi kuchisandutsa mtembo. Mudabalalitsa adani anu ndi mkono wanu wamphamvu.

Zakumwamba ndi zanu, dziko lapansi nalonso ndi lanu. Mudapanga dziko lonse ndi zonse zam'menemo.

Mudalenga kumpoto ndi kumwera. Mapiri a Tabori ndi Heremoni akukutamandani ndi chimwemwe.

Inu muli ndi mphamvu zonse. Dzanja lanu ndi lamphamvu kwambiri, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.

Maziko a ufumu wanu ndiwo kulungama ndi kuweruza mosakondera. Mumaonetsa chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika pa zonse zimene mumachita.

Ngodala anthu amene mumaŵaphunzitsa kuimba nyimbo zachikondwerero, amene amayenda m'chikondi chanu, Inu Chauta.

Iwowo amakondwa masiku onse chifukwa cha Inu, ndipo amatamanda kulungama kwanu.

Amanyadira ulemerero wanu ndi mphamvu zanu. Mphamvu zathu zalimba chifukwa mwatikomera mtima.

Chauta ndiye chishango chathu, Woyera wa Israele ndiye mfumu yathu.

Kale mudalankhula m'masomphenya kwa anthu anu okhulupirika, mudati, “Ndamuveka chisoti chaufumu munthu amene ali wamphamvu, ndamukweza amene ali wosankhidwa pakati pa anthu.

Chikondi chanu chosasinthika chakhazikika kuti chikhale mpaka muyaya, kukhulupirika kwanu nkwachikhalire ngati mlengalenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:8-9

Chauta ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi chosasinthika.

Chauta ndi wabwino kwa onse, amachitira chifundo zamoyo zonse zimene adazilenga.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:6

Paja m'Malembo mudalembedwa kuti. “Ndasankha mwala wamtengowapatali. Ndikuuika tsopano m'Ziyoni, ngati mwala wapangodya. Wokhulupirira Iye sadzachita manyazi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 2:19-20

Nchifukwa chake tsono, inu amene simuli Ayuda, sindinunso alendo kapena akudza ai, koma ndinu nzika pamodzi ndi anthu ake a Mulungu, ndiponso ndinu a m'banja lake la Mulungu.

Pa nthaŵi imeneyo, munkayenda m'zoipa potsata nzeru zapansipano, ndipo munkamvera mkulu wa aulamuliro amumlengalenga. Mkuluyo ndi mzimu woipa umene ukugwira ntchito tsopano pakati pa anthu oukira Mulungu.

Ndinu omangidwa pamodzi m'nyumba yomangidwa pa maziko amene ndi atumwi ndi aneneri, ndipo Khristu Yesu mwini ndiye mwala wapangodya.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 26:3-4

Inu Chauta, mumapatsa mtendere weniweni kwa amene ali ndi mtima wokhazikika, chifukwa chokhulupirira Inu.

Inu anthu, mukhulupirire Chauta mpaka muyaya, chifukwa chakuti Chauta Mulungu ndiye thanthwe losatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 144:2

Ndiye thanthwe langa ndi tchemba langa londiteteza, ndiye linga langa londipulumutsa, ndiye chishango changa chothaŵirako. Amaika mitundu ya anthu mu ulamuliro wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 146:5-6

Ngwodala munthu amene chithandizo chake chimafumira kwa Mulungu wa Yakobe, munthu amene amakhulupirira Chauta, Mulungu wake.

Chauta adalenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili m'menemo. Amasunga malonjezo ake nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 104:18

M'mapiri aatali ndimo m'mene mumakhala mbalale, m'matanthwe ndimo m'mene mumathaŵira mbira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 8:14

ndiye adzakhala ngati malo opatulika. Koma kwa anthu a ku Yuda ndi a ku Israele adzakhala ngati mwala wokhumudwitsa, ndiponso ngati thanthwe logwetsetsa. Kwa anthu a mu Yerusalemu, adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 30:5

Mau aliwonse a Mulungu ndi oona. Iye ndiye chishango choteteza amene amathaŵira kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 9:10

Amene amadziŵa dzina lanu, Inu Chauta, amakukhulupirirani, pakuti Inu Chauta simuŵasiya anthu okufunitsitsani.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 62:1

Mtima wanga umakhala chete kuyembekezera Mulungu yekha, pakuti chipulumutso changa chimafumira kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 50:7

Koma kunyoza kwao sindikuvutika nako, chifukwa Ambuye Chauta amandithandiza. Nchifukwa chake ndalimbitsa mtima wanga ngati mwala. Ndikudziŵa kuti sadzandichititsa manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 107:6

Tsono anthu aja adalira kwa Chauta pamene anali m'mavuto amenewo, ndipo Chauta adaŵapulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:6

Sindikayika konse kuti Mulungu, amene adayamba kuchita ntchito yabwinoyi mwa inu, adzaipitiriza mpaka itatsirizika pa Tsiku la Kubweranso kwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:19

Ndi waukulu ubwino wanu umene mwaŵasungira anthu okumverani, umene mwaŵachitira anthu othaŵira kwa Inu, aliyense waona zimenezi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 30:6

Davide adavutika koopsa, pakuti anthu ankakamba zoti amponye miyala, chifukwa cha chisoni chao pokumbukira ana ao aamuna ndi aakazi. Koma Davide adapeza mphamvu mwa Chauta, Mulungu wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 52:12

Koma ulendo uno simudzachoka mofulumira, simudzachita chothaŵa. Chauta azidzayenda patsogolo panu, Mulungu wa Aisraele azidzakutetezani kumbuyo kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 1:3-4

Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu. Ndiwo Atate a chifundo ndi otilimbitsa mtima kwathunthu.

Mulungu amatilimbitsa mtima m'masautso athu onse, kuti monga momwe Iye amalimbitsira ife mtima, nafenso tithe kuŵalimbitsa mtima anzathu amene ali pakati pa masautso amitundumitundu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:20-22

Mitima yathu ikuyembekeza Chauta, chifukwa Iye ndiye chithandizo ndi chishango chathu.

Mitima yathu imasangalala mwa Chauta, popeza kuti timadalira dzina lake loyera.

Inu Chauta, chikondi chanu chosasinthika chikhale pa ife, chifukwa timakhulupirira Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 56:3-4

Pamene ndichita mantha ndimadalira Inu.

Ndimatamanda Mulungu chifukwa cha zimene wandilonjeza. Ndimakhulupirira Mulungu mopanda mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:114

Inu ndinu malo anga obisalako ndiponso chishango changa, ndimakhulupirira mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 146:1-2

Tamandani Chauta! Tamanda Chauta, iwe mtima wanga.

Chauta adzakhala mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako, iwe Ziyoni, adzalamulira ku mibadwo yonse. Tamandani Chauta!

Ndidzatamanda Chauta pa moyo wanga wonse. Ndidzaimba nyimbo zotamanda Mulungu wanga nthaŵi zonse pamene ndili moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 4:8-9

Tikuwona masautso a mtundu uliwonse, koma osapsinjidwa. Tikuthedwa nzeru, koma osataya mtima.

Adani akutizunza, koma sitisoŵa wotithandiza. Akutigwetsa pansi, koma sitikugonja.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:8

Yesu Khristu ndi yemweyo dzulo, lero ndi mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 16:18

Ndipo Ine ndikuti, Ndiwe Petro, ndipo pa thanthwe limeneli ndidzamanga Mpingo wanga. Ndipo ngakhale mphamvu za imfa sizidzaugonjetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 10:11

Paja Malembo akuti, “Munthu aliyense wokhulupirira Iye, sadzachita manyazi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 121:1-2

Ndimakweza maso anga ku mapiri. Kodi chithandizo changa chimachokera kuti?

Chithandizo changa nchochokera kwa Chauta, amene adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 32:15

Yesuluni, anthu ake a Chauta adakulupala, koma iwowo adamuukira, adanenepa ndi kukula thupi, ndipo adakhuta zedi, kenaka adasiya Mulungu Mlengi wao, nanyoza mtetezi ndi mpulumutsi wao.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 17:6

Ine ndidzakhala patsogolo pako kumeneko pafupi ndi thanthwelo, pa phiri la Horebu. Ukamenye thanthwe, tsono mudzatuluka madzi m'thanthwemo, kuti anthuwo amwe.” Mose adachitadi zimenezo pamaso pa atsogoleri a Aisraele aja.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 32:13

Adaŵathandiza kuti azilamula maiko amapiri, ndipo adadya zomera zam'minda. Adaŵadyetsa uchi wam'mathanthwe, ndi mafuta ochokera m'nthaka yamiyala.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 48:21

Pamene ankatsogolera anthu ake m'chipululu, iwo sadamve ludzu. Adaŵapatsa madzi otuluka m'thanthwe. Adang'amba thanthwelo, ndipo mudatuluka madzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 107:28-30

Tsono anthu aja adalira kwa Chauta pamene anali m'mavuto amenewo, ndipo Chauta adaŵapulumutsa ku mavuto aowo.

Chauta adatontholetsa namondwe, ndipo mafunde apanyanja adachita bata.

Waŵasonkhanitsa kuchokera ku maiko onse, kuchokera kuvuma ndi kuzambwe, kumpoto ndi kumwera.

Choncho anthuwo adasangalala chifukwa kudachita bata, ndipo Chauta adakaŵafikitsa kudooko kumene ankalinga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 19:25

“Mtheradi ndikudziŵa kuti Momboli wanga alipo, ndipo pa nthaŵi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 18:50

Mulungu amathandiza mfumu yake, kuti izipambana nthaŵi ndi nthaŵi. Amaonetsa chikondi chake chosasinthika kwa wodzozedwa wake, ndiye kuti kwa Davide ndi kwa zidzukulu zake mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:8

Mau a Mulungu akutinso, “Umenewu ndi mwala wokhumudwitsa anthu, ndi thanthwe loŵagwetsa.” Amakhumudwa popeza kuti amakana kumvera mau a Mulungu, ndipo anali oyeneradi kuti adzaone zotere.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 45:22

“Inu anthu onse a pa dziko lapansi, tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke. Paja Ine ndine Mulungu, palibenso wina ai.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:1

Bwerani, timuimbire Chauta. Tiyeni tifuule ndi chimwemwe kwa Iye, thanthwe lotipulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 14:1

Yesu adauza ophunzira akewo kuti “Mtima wanu usavutike. Khulupirirani Mulungu, khulupirirani Inenso.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 61:1-2

Inu Mulungu, imvani kulira kwanga, mverani pemphero langa.

Ine wokhala ku mathero a dziko lapansi, ndataya mtima, ndipo ndikuitana Inu. Munditsogolere ku thanthwe lalitali.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:5-6

Udzipereke m'manja mwa Chauta, umukhulupirire ndipo Iye adzakusamalira.

Adzaonetsa poyera kusalakwa kwako, ndipo kulungama kwako kudzaŵala ngati usana.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 20:7

Ena amatamira magaleta ankhondo, ena amadalira akavalo, koma ife timatamira dzina la Chauta, Mulungu wathu, timamutama Iyeyo mopemba.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:23

Tilimbikire kuvomereza mosafookera zimene timaziyembekeza, pakuti Iye amene adatilonjeza zimenezi ngwokhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo