Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

108 Mauthenga a Baibulo Okhudza Mimba

Mulungu amafuna kukhala nawe pa chilichonse chimene ukuchita. Afuna ukhale ndi chikhulupiriro chonse kuti Atate akuyang’anira zinthu zonse zazing’ono ndi zazikulu m’moyo wako.

Pa nthawi yokongola iyi m’moyo wako, uli ndi dalitso lalikulu, mphatso yapadera yomwe uyenera kuisamalira ndi kuikonda kwambiri. Uyenera kuisamalira kuti ikule bwino, ukhale woleza mtima ndipo uiiyetse mwanzeru pamene ikukula.

Kukhala ndi pakati kukubweretsera chimwemwe chachikulu, chifukwa uli ndi munthu amene akukufuna tsiku lililonse. Muzipsompsona, muziimbira nyimbo, ndipo muzipempherera.

Sangalala ndi gawo lililonse la mimba yako ndipo ukhale ndi chiyembekezo kuti zonse zidzayenda bwino. Lankhula ndi Mzimu Woyera, umupemphe kuti akuthandize pa mantha ako ndi kukupatsa mphamvu pa nthawi yobereka.

Mwana akangobadwa, yamikani Mulungu ndipo sangalalani ndi mphindi iliyonse naye. Kubweretsa moyo padziko lapansi ndi mphatso yochokera kwa Mulungu.


Yohane 16:21

Pa nthaŵi yochira mai amavutika chifukwa nthaŵi yake yafika. Koma pamene wabadwa mwana, saganizakonso za kuzunzikako, chifukwa cha chimwemwe chakuti kunja kuno kwabadwa mwana.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:13

Paja ndinu mudapanga za m'kati mwanga, mudandiwumba m'mimba mwa amai anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 127:3

Zoonadi, ana ndi mphatso yochokera kwa Chauta, zidzukulu ndi mphotho yake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:13-14

Paja ndinu mudapanga za m'kati mwanga, mudandiwumba m'mimba mwa amai anga.

Ndikukutamandani, Inu oopsa ndi odabwitsa. Ntchito zanu zonse nzodabwitsa. Mumandidziŵa bwino kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 25:21

Tsono poti mkazi wa Isaki anali wosabereka, Isakiyo adapempherera mkazi wake kwa Chauta. Chauta adamva pemphero lake, ndipo Rebeka adatenga pathupi.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 4:1

Adamu adakhala ndi mkazi wake Heva ndipo mkaziyo adatenga pathupi. Tsono adabala mwana wamwamuna, ndipo adati, “Ndalandira mwana wamwamuna mwa chithandizo cha Chauta.” Motero mwanayo adamutcha Kaini.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 1:5

“Ndisanakulenge m'mimba mwa mai wako, ndinali nditakudziŵa kale. Usanabadwe nkomwe, ndinali ntakupatula kale, ndidakuika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 30:22-23

Tsono Mulungu adakumbukira Rakele, namva pemphero lake, nkulola kuti abale ana.

Iyenso adatenga pathupi, nabala mwana wamwamuna. Ndipo adati, “Mulungu wandichotsa manyazi a uchumba wanga.”

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:27-28

Motero Mulungu adalenga munthu, m'chifanizo chake, adaŵalengadi m'chifanizo cha Mulungu. Adaŵalenga wina wamwamuna wina wamkazi.

Adaŵadalitsa poŵauza kuti, “Mubereke ndi kuchulukana, mudzaze dziko lonse lapansi ndi kumalilamulira. Ndakupatsani ulamuliro pa nsomba, mbalame ndi nyama zonse zimene zikukhala pa dziko lapansi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 1:24-25

Pambuyo pake mkazi wake Elizabeti adatenga pathupi, nabindikira miyezi isanu.

Adati, “Ambuye andichitira zotere: nthaŵi inoyi andiwonetsa chifundo chao, andichotsa manyazi pakati pa anthu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 44:24

Chauta, Mpulumutsi wako, amene adakupanga m'mimba mwa mai wako, akunena kuti, “Ndine Chauta, amene ndidapanga zinthu zonse. Pamene ndinkayalika zakuthambo, ndinali ndekha. Pamene ndinkalenga dziko lapansi, kodi analipo amene adandithandiza?

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 1:36-37

“Onani, mbale wanu uja Elizabeti, nayenso akuyembekezera mwana wamwamuna mu ukalamba wake. Anthu amati ngwosabala, komabe uno ndi mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.

Pajatu palibe kanthu kosatheka ndi Mulungu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 1:41-44

Pamene Elizabeti adamva malonje a Maria, mwana adayamba kutakataka m'mimba mwake. Elizabeti adadzazidwa ndi Mzimu Woyera,

ndipo adalankhula mokweza mau kuti, “Ndinu odala kupambana akazi ena onse, ngwodalanso Mwana wanu.

Ine ndine yani kuti inu, mai wa Ambuye anga, mudzandiyendere?

Chifukwatu pamene ndinamva malonje anu, mwana anayamba kutakataka ndi chimwemwe m'mimba mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 11:11

Pokhala ndi chikhulupiriro, Sara yemwe adalandira mphamvu zakutenga pathupi, ngakhale zaka zake zakubala mwana zinali zitapita kale. Zimenezi zidatheka chifukwa adaavomera kuti amene adazilonjezayo ngwokhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 29:35

Adatenganso pena pathupi, nabala mwana winanso wamwamuna, ndipo adati, “Tsopano ndidzatamanda Chauta.” Motero mwanayo adamutcha Yuda. Apo adayamba walekeza kubala.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 3:16

Pambuyo pake Mulungu adauza mkaziyo kuti, “Ndidzaonjeza zovuta zako pamene udzakhala ndi pathupi, udzamva zoŵaŵa pa nthaŵi yako ya kubala mwana. Udzakhumba mwamuna wako, ndipo mwamuna wakoyo adzakulamulira iwe.”

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 35:17

Zidafika poipa kwambiri, ndipo mzamba adamuuza kuti, “Musaope, ameneyu ndi mwana wina wamwamuna.”

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 1:20

Motero Hana adaima, ndipo adabala mwana wamwamuna namutcha dzina loti Samuele, kunena kuti, “Ndidachita kumpempha kwa Chauta.”

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 1:36

“Onani, mbale wanu uja Elizabeti, nayenso akuyembekezera mwana wamwamuna mu ukalamba wake. Anthu amati ngwosabala, komabe uno ndi mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:28

Adaŵadalitsa poŵauza kuti, “Mubereke ndi kuchulukana, mudzaze dziko lonse lapansi ndi kumalilamulira. Ndakupatsani ulamuliro pa nsomba, mbalame ndi nyama zonse zimene zikukhala pa dziko lapansi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 113:9

Amapatsa banja mkazi wosabala, namsandutsa mai wosangalala wa ana. Tamandani Chauta!

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 1:27-28

Mwana uyu ndidachita kupempha, ndipo Chauta wandipatsa chopempha changacho.

Nchifukwa chake ndampereka kwa Chauta. Moyo wake wonse mwanayu adzakhala wake wa Chauta.” Ndipo onsewo adapembedza Chauta kumeneko.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 128:3

Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka, m'kati mwa nyuma yako. Ana ako adzakhala ngati tiziphukira taolivi, kuzungulira tebulo lako.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 23:26

Palibe mkazi amene adzapititse padera m'dziko mwanumo, ndipo wosabala sadzaoneka. Ndidzakupatsani moyo wautali.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 126:3

Ndithudi, Chauta watichitira zazikulu, ndipo tasangalala.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 1:20-21

Akulingalira zimenezi, mngelo wa Ambuye adamuwonekera m'maloto, namuuza kuti, “Yosefe, mwana wa Davide, usaope kumtenga Maria, mkazi wakoyu. Pathupi ali napopa padachitika ndi mphamvu za Mzimu Woyera.

Adzabala mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha dzina lake Yesu, chifukwa adzapulumutsa anthu ake ku machimo ao.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 49:1

Mverani inu anthu a ku maiko a m'mphepete mwa nyanja, tcherani khutu, inu anthu akutali. Chauta adandiitana ndisanabadwe, adanditchula dzina ndidakali m'mimba mwa amai anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 4:19

Inu ana anga, monga mkazi amamva zoŵaŵa pochira, inenso ndikumva zoŵaŵa chifukwa cha inu mpaka moyo wa Khristu ukhazikike mwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 1:16

“Mukamathandiza azimai achihebri pochira, akabadwa mwana wamwamuna, mupheni, akakhala wamkazi, mlekeni.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:16

Maso anu adandiwona ndisanabadwe. Masiku a moyo wanga mudaŵalemberatu m'buku mwanu, asanayambe nkuŵerengedwa komwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 2:7

ndipo adabala mwana wake wachisamba wamwamuna. Adamkulunga m'nsalu namgoneka m'chodyera cha zoŵeta, chifukwa adaasoŵa malo m'nyumba ya alendo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:31

Nanga tsono tinganenenso chiyani pa zonsezi? Ngati Mulungu ali pa mbali yathu, angatsutsane nafe ndani?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 71:6

Inu mwakhala wondichirikiza kuyambira pa nthaŵi imene ndidabadwa. Inu ndinu amene mudanditulutsa m'mimba mwa mai wanga. Ndimatamanda Inu nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:7

Mngelo wa Chauta amatchinjiriza anthu omvera Iye, ndipo amaŵapulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:6

Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ulemerero wa ana ndi atate ao.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 19:14

Koma Yesu adati, “Alekeni anaŵa azibwera kwa Ine, musaŵaletse. Paja Ufumu wakumwamba ndi wa anthu otere.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:11

Adzasamala nkhosa zake ngati mbusa. Adzasonkhanitsa anaankhosa ndi kuŵakumbatira. Ndipo adzatsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:9

Chauta ndi wabwino kwa onse, amachitira chifundo zamoyo zonse zimene adazilenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 21:1-2

Chauta adakumbukira Sara namchitira zimene adaamulonjeza.

Sara ataona, adauza Abrahamu kuti, “Mchotseni mdzakaziyu pamodzi ndi mwana wake yemweyu. Mwana wa mdzakazi asadzalandireko chuma chanu chimene adzalandire mwana wanga Isaki.”

Zimenezi zidamuvuta kwambiri Abrahamu, chifukwa chakuti Ismaele nayenso anali mwana wake.

Koma Mulungu adauza Abrahamu kuti, “Mtima wako usavutike chifukwa cha mwanayo ndi mzikazi wako Hagara. Zonse zimene akukuuza Sara uchite, chifukwa Isakiyu ndi amene adzakhala kholo la zidzukulu zako monga momwe ndidakulonjezera.

Mwana wa mdzakaziyunso ndidzampatsa ana ambiri, ndipo adzasanduka mtundu ndithu, popeza kuti iyeyunso ndi mwana wako.”

M'maŵa mwake, m'mamaŵa, Abrahamu adapatsa Hagara chakudya ndi thumba lachikopa la madzi. Kenaka adatenga mwanayo nabereketsa Hagara, ndipo atatero adamuuza kuti azipita. Hagara adachokadi, nkumangoyendayenda m'chipululu cha Beereseba.

Tsono madzi aja atamthera, adangosiya mwanayo pa chitsamba.

Iye adakakhala pansi poteropo, pa mtunda wa mamita 100, chifukwa ankati, “Ine sindingathe kumaonerera mwana wanga alikufa chotere.” Ali pansi pomwepo, mwanayo adayamba kulira.

Mulungu adamumva mwanayo akulira, ndipo mngelo wa Mulungu adalankhula ndi Hagara kuchokera kumwamba, adati, “Kodi iwe Hagara, chikukuvuta nchiyani? Usachite mantha. Mulungu wamva kulira kwa mwanayu.

Dzuka, pita, ukamnyamule ndi kumgwiritsa ndi dzanja lako. Zidzukulu zako zidzakhala mtundu waukulu.”

Apo Mulungu adatsekula maso a Hagara, ndipo adaona chitsime. Iye adapita pachitsimepo, nakadzaza thumba lachikopa lija ndi madzi, nkumwetsako mwanayo.

Choncho Sarayo adatenga pathupi, nabalira Abrahamu mwana wamwamuna pamene Abrahamuyo anali nkhalamba. Mwana ameneyu adabadwa pa nthaŵi yeniyeni imene Mulungu adaanena.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:15

Mapangidwe anga sadabisike pamaso panu pamene ndinkapangidwa mwachinsinsi, pamene ndinkaumbidwa mwaluso m'mimba mwa amai anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 127:4-5

Ana apaunyamata ali ngati mivi m'manja mwa munthu wankhondo.

Ngwodala amene phodo lake nlodzaza ndi mivi yotere. Sadzamchititsa manyazi akamalankhula ndi adani ake pa bwalo lamilandu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:17-18

Koma chikondi cha Chauta nchamuyaya kwa anthu omumvera, zidzukulu zao zonse amazichitira zolungama.

Anthuwo ndi amene amasunga chipangano chake, amene amakumbukira kusunga malamulo ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 66:9

Kodi ine ndidzafikitsa anthu anga mpaka nthaŵi yobala, koma osalola kuti abaledi?” Akuterotu Chauta. “Kodi Ine, amene ndili wobalitsa, ndingatseke mimba nthaŵi imeneyo?” Akuterotu Mulungu wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:73

Manja anu adandilenga ndi kundiwumba. Patseni nzeru zomvetsa, kuti ndiziphunzira malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 1:57-58

Nthaŵi yakuti Elizabeti achire idakwana, ndipo adabala mwana wamwamuna.

Anzake ndi abale ake atamva kuti Ambuye amchitira chifundo chachikulu chotere, adakondwera naye pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 30:1-2

Rakele ataona kuti sakumubalira ana Yakobe, adayamba kuchita nsanje ndi mkulu wake uja, ndipo adauza Yakobe kuti, “Mundipatse ana, apo ai, ndingofa basi.”

Ndipo Zilipa adabala mwana wamwamuna.

Tsono Leya adati, “Ndachita mwai.” Motero mwanayo adamutcha Gadi.

Zilipa mdzakazi wa Leyayo adamubaliranso Yakobe mwana wamwamuna wachiŵiri.

Apo Leya adati, “Ndakondwa! Ndipo akazi adzanditchula wamwai.” Motero mwanayo adamutcha Asere.

Pa nthaŵi yodula tirigu, Rubeni adapita ku minda, nakapezako zipatso za mankhwala a chisulo, ndipo adadzapatsa Leya mai wake. Rakele adauza Leya kuti, “Chonde patseko mankhwala amene mwana wako wakufuniraŵa.”

Leya adayankha kuti, “Kodi sunakhutitsidwebe ndi mwamuna wanga udandilandayu? Tsopano ufuna kutenganso mankhwala a chisulo amene mwana wanga wandifunira?” Rakele adati, “Ukandipatsa mankhwala a chisulo ochokera kwa mwana wakoŵa, ŵamunaŵa akhala ndi iwe usiku uno.”

Pamenepo Yakobe ankabwera madzulo kuchokera ku munda, Leya adatuluka kukamlonjera, nati “Lero mugone kunyumba kwanga kuno, chifukwa cha mankhwala a chisulo ondifunira mwana wanga.” Motero Yakobe adakhala ndi Leya usiku umenewo.

Mulungu adamva pemphero la Leya, choncho adatenga pathupi, namubalira Yakobe mwana wamwamuna wachisanu.

Tsono adati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa ndidapereka mdzakazi wanga kwa mwamuna wanga.” Motero mwanayo adamutcha Isakara.

Leya adatenganso pena pathupi, namubalira Yakobe mwana wamwamuna wachisanu ndi chimodzi.

Yakobe adapsera mtima Rakele, namuuza kuti, “Sindingathe kuloŵa m'malo mwa Mulungu. Iyeyo ndiye akukuletsa kubala ana.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:26

Munthu woopa Chauta ali ndi chikhulupiriro cholimba, ndipo ana ake adzakhala napo pothaŵira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 51:5

Zoonadi, ndidabadwa mu uchimo, ndinali mu uchimo kuyambira pamene mai wanga adatenga pathupi pa ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 18:15-16

Anthu ena ankabwera ndi ana omwe kwa Yesu kuti aŵakhudze. Ophunzira ake poona zimenezi, ankaŵazazira.

Koma Yesu adaŵaitana nati, “Alekeni anaŵa azibwera kwa Ine, musaŵaletse. Paja Ufumu wa Mulungu ndi wa anthu otere.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 8:5

Ndiyetu mudamlenga mochepera pang'ono kwa Mulungu amene, mudampatsa ulemerero ndi ulemu wachifumu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:7

Inunso amuna, muzikhala moŵamvetsa bwino akazi anu. Muziŵachitira ulemu popeza kuti iwowo ndi mtundu wofookerapo, ndiponso ngolandira nanu pamodzi mphatso ya Mulungu, imene ili moyo wosatha. Muzitero, kuti pasakhale kanthu koletsa mapemphero anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 29:31

Chauta ataona kuti Yakobe sankakonda kwambiri Leya, adalola kuti Leyayo abale ana, koma Rakele ai.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 138:8

Chauta adzaona kuti cholinga chake pa ine chichitikedi. Chikondi chanu, Inu Chauta, nchamuyaya. Muipitirize ntchito imene mwaiyambayo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:13

Mulungu amene amatipatsa chikhulupiriro, adzaze mitima yanu ndi chimwemwe ndi mtendere pakumvera Iye, kuti chiyembekezo chanu chizikulirakulira ndi mphamvu za Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:15

Maso onse amayang'anira kwa Inu, ndipo mumaŵapatsa chakudya pa nthaŵi yake.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 20:12

“Uzilemekeza atate ndi amai ako, kuti masiku a moyo wako achuluke m'dziko limene Chauta, Mulungu wako, akukupatsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:2

Muzifunafuna za Kumwamba, osati zapansipano.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 16:11

Mumandiwonetsa njira ya ku moyo. Ndimapeza chimwemwe chachikulu kumene kuli Inu, ndidzasangalala mpaka muyaya ku dzanja lanu lamanja.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:26

Onani mbalame zamumlengalenga. Sizifesa kapena kukolola kapena kututira m'nkhokwe ai. Komabe Atate anu akumwamba amazidyetsa. Nanga inu sindinu amtengowapatali kuposa mbalame?

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 54:1

“Fuula ndi chimwemwe iwe Yerusalemu amene wakhala ngati chumba chopanda ana, fuula mosangalala, iwe amene sudamvepo zoŵaŵa za kubala. Pakuti tsopano udzakhala ndi ana ochuluka kuposa mkazi amene sadasiyidweko ndi mwamuna wake,” akuterotu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 107:41

Koma anthu osoŵa adaŵatulutsa m'mavuto ao, adachulukitsa mabanja ao ngati magulu a nkhosa.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:22

Koma zipatso zimene Mzimu Woyera amabweretsa m'moyo wa munthu ndi izi: Chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, kukhulupirika,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:4

Kondwa mwa Chauta, ndipo adzakupatsa zimene mtima wako ukukhumba.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 1:30-31

Mngeloyo adamuuza kuti, “Musaope, Maria, Mulungu wakukomerani mtima.

Mudzatenga pathupi, ndipo mudzabala mwana wamwamuna. Mudzamutcha dzina lake Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:5

Inu Chauta, Mulungu wanga, mwatichitira zodabwitsa zambiri, mwatikonzera zabwino zambiri zakutsogolo. Palibe ndi mmodzi yemwe wotha kulingana nanu. Ndikati ndisimbe ndi kulongosola za zimenezo, sindingathe kuziŵerenga zonse chifukwa cha kuchuluka kwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:165

Anthu okonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, palibe china chotha kuŵagwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 29:17

Uzimlanga mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere mu mtima, adzakondweretsa mtima wako m'tsogolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:11

Pakuti Chauta ndiye dzuŵa ndi chishango, amatichitira chifundo ndi kutipatsa ulemu. Chauta saŵamana zabwino anthu oyenda molungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 61:10

Tsono ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Chauta, mtima wanga ukukondwadi chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso. Wandiveka mkanjo wa chilungamo. Zinali ngati mkwati wamwamuna wavala nkhata ya maluŵa m'khosi, ndiponso ngati mkwati wamkazi wavala mikanda ya mtengo wapatali.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 29:11

Chauta amapatsa anthu ake mphamvu. Amaŵadalitsa anthu ndi mtendere. Salmo la Davide. Nyimbo yoimba potsekula Nyumba ya Mulungu

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:24

Njira yopita ku moyo imakamufikitsa ku ntchito zangwiro, kuti alewe malo a anthu akufa kunsiko.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 22:31

Adzalalika za chipulumutso chake kwa anthu amene mpaka tsopano sanabadwe, ponena kuti Chauta ndiye adapulumutsa anthu ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 18:10

“Chenjerani kuti musanyoze ndi mmodzi yemwe mwa anaŵa. Ndithu ndikunenetsa kuti angelo ao Kumwamba amakhala pamaso pa Atate anga amene ali Kumwambako nthaŵi zonse.” [

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:2

Musamatsanzira makhalidwe a anthu odalira zapansipano, koma Mulungu asinthe moyo wanu wonse pakukupatsani mitima yatsopano. Pamenepo mudzatha kudziŵa zimene Mulungu afuna, ndipo mudzazindikira zimene zili zabwino, zangwiro ndi zomkondwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 21:6-7

Tsono Sara adati, “Mulungu wandikondweretsa ndi kundiseketsa. Aliyense amene adzamve zimenezi, adzakondwera nane.”

Ndipo adati, “Akadadziŵa ndani kuti Sara nkuyamwitsa mwana? Komabe ndamubalira mwana wamwamuna Abrahamu pamene ali nkhalamba.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 56:13

Pakuti mwalanditsa moyo wanga ku imfa. Inde mwandichirikiza mapazi kuti ndisagwe, kuti motero ndiziyenda pamaso pa Mulungu m'kuŵala kwa amoyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:3

Akuchiritsa a mtima wachisoni, ndipo akumanga mabala ao.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:6-7

Musade nkhaŵa ndi kanthu kalikonse, koma m'mapemphero anu onse muzipempha Mulungu zimene zikusoŵani, ndipo nthaŵi zonse muzipemphe ndi mtima woyamika.

Pamenepo mtendere wochokera kwa Mulungu, umene uli wopitirira nzeru zonse za anthu, udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 66:13

Ndidzakusangalatsani ku Yerusalemu monga momwe mai amasangalatsira mwana wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 130:5

Ndimayembekeza chithandizo cha Chauta, ndimayembekeza ndi mtima wonse, ndipo ndimakhulupirira mau ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:18

Chauta amakhala pafupi ndi anthu a mtima wosweka, amapulumutsa otaya mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:30

Tsono ngati Mulungu amaveka motere udzu wakuthengo, umene ungokhalapo lero lokha, maŵa lino nkuponyedwa pa moto, nanji inuyo, angapande kukuvekani, inu a chikhulupiriro chochepanu?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:16

Mumafumbatula dzanja lanu, ndipo mumapatsa chamoyo chilichonse zofuna zake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:31

Koma amene amakhulupirira Chauta adzalandira mphamvu zatsopano, adzauluka ngati ziwombankhanga. Adzathamanga koma osatopa, adzayenda koma osalefuka konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:92

Malamulo anu akadapanda kundisangalatsa, bwenzi nditafa ndi mazunzo anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:3

Ndiye amene amakhululukira machimo ako onse, ndi kuchiritsa matenda ako onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 66:19

Koma zoonadi, Mulungu wandimvera, wasamala mau a pemphero langa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 43:4

Popeza kuti ndiwe wanga wapamtima, ndidzapereka anthu m'malo mwa iwe. Chifukwa ndiwe wamtengowapatali pamaso panga, ndipo ndimakukonda, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 18:10

Chauta adati, “Ndikukulonjeza kuti pakapita miyezi isanu ndi inai ndidzabweranso, ndipo mkazi wako adzakhala ali ndi mwana wamwamuna.” Sara ankangomvetsera ali kuseri kwa chitseko cha hema.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:15

Masiku anga ali m'manja mwanu. Pulumutseni kwa adani anga ndi kwa ondizunza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 135:4

Wadzisankhulira Yakobe kuti akhale wake, Israele kuti akhale chuma chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:28

Ndipo tikudziŵa kuti Mulungu amayendetsa zinthu mwa njira yoti zonse ziŵakomere anthu omukonda ndipo apindulepo. Anthuwo ndi amene Iye amaŵaitana monga momwe Iye adazikonzera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 73:26

Thupi langa ndi mtima wanga zingafooke chotani, Mulungu ndiye mphamvu za mtima wanga ndiyenso wondigaŵira madalitso mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 130:7

Iwe Israele, khulupirira Chauta. Paja Chauta ndi wa chikondi chosasinthika, ndi wokonzeka kupulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 41:10

Usachite mantha chifukwa Ine ndili nawe, usataye mtima, poti Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu, ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 71:5

Inu Ambuye, ndinu amene ndimakukhulupirirani, Inu Chauta, ndinu amene ndimakudalirani kuyambira ubwana wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:1

Onani kukula kwake kwa chikondi chimene Atate adatikonda nacho. Adatikonda kwambiri, kotero kuti timatchedwa ana a Mulungu. Ndipo ndifedi ana ake. Anthu odalira zapansipano satidziŵa ifeyo, chifukwa Iyeyonso sadamdziŵe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 28:7

Chauta ndiye mphamvu zanga, ndiyenso chishango changa chonditeteza. Ndaika mtima wanga wonse pa Iye. Wandithandiza, choncho mtima wanga ukusangalala, ndipo ndimamthokoza ndi nyimbo yanga.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 2:21

Chauta adadalitsadi Hana, ndipo adabala ana aamuna atatu ndi ana aakazi aŵiri. Ndipo mnyamata uja Samuele ankakula akutumikira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:114

Inu ndinu malo anga obisalako ndiponso chishango changa, ndimakhulupirira mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 29:32

Leya adatenga pathupi, ndipo adabala mwana wamwamuna. Tsono adati, “Chauta waona zovuta zanga. Ndithu tsopano mwamuna wanga adzayamba kundikonda.” Motero mwanayo adamutcha Rubeni.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:17

Sindidzafa, ndidzakhala moyo, ndipo ndidzalalika ntchito za Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:19

Amene amamvera Chauta, amaŵapatsa zofuna zao, amamvanso kulira kwao, naŵapulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 28:20

Muzikaŵaphunzitsa kusunga zonse zimene Ine ndidakulamulani. Ndipo Ineyo ndili nanu masiku onse, mpaka kutha kwa dziko lino lapansi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 146:9

Chauta amateteza alendo, amachirikiza mkazi wamasiye ndiponso mwana wamasiye. Koma njira za anthu oipa amazipotoza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:28

Ndafookeratu ndi chisoni. Limbitseni monga momwe mudalonjezera.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye, ndinu Alfa ndi Omega! Atate, mlengi wa thambo ndi dziko lapansi, ndinu woyamba ndi wotsiriza, chiyambi ndi chimaliziro. Atate pakali pano ndikubwera kwa inu m'dzina la Yesu kuti ndikuthokozani ndi mtima wanga wonse chifukwa cha mimba yanga, chifukwa mwasankha kundipatsa dalitso lokongola komanso losangalika lomwe nthawi yomweyo ndi udindo waukulu, zikomo chifukwa chopeza chisomo pamaso panu ndipo mwandisankha kukhala chida chobweretsera mwana uyu wodabwitsa padziko lapansi amene akukula m'mimba mwanga. Mulungu wokondedwa tambasulani dzanja lanu pa ine kuti ndimve mtendere ndi mpumulo pakati pa gawo lino, mawu anu amati: "Sipadzakhala mkazi amene adzataya mimba, kapena wosabala m'dziko lanu; ndipo Ine ndidzakwaniritsa masiku anu," chifukwa chake, ndimakhulupirira kuti mumasamalira miyoyo yathu ndipo mumasamalira thanzi la mwana wanga. Atate ndikuyika chitukuko, kukula ndi ubwino wa mwana wanga m'manja mwanu, ndikupemphani kuti mumupange kukhala munthu wabwino, wakhama, wolimba mtima, wachilungamo wodzala ndi chisomo ndi chiyanjo chanu. Mundipatse nzeru kuti ndimulangize m'njira yanu ndipo akule poopa dzina lanu, Mulungu ndithandizeni kukhala mawu olimbikitsa ndi uphungu kwa iye. M'dzina la Yesu, Ameni!