Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -


100 Mau a Mulungu Okhudza Kukhala Owona Mtima

100 Mau a Mulungu Okhudza Kukhala Owona Mtima


1 Timoteyo 1:5

Cholinga changa pokupatsa malangizo ameneŵa, nchakuti pakhale chikondi chochokera mu mtima woyera, mu mtima wopanda kanthu koutsutsa, ndiponso m'chikhulupiriro chopanda chiphamaso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:3

Khalidwe la kudzipereka ndi kukhulupirika zisakuthaŵe, makhalidwe ameneŵa uziyenda nawo ngati mkanda wam'khosi, uŵalembe mumtima mwako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:2

Ntchito zake za munthu zimakhala zolungama pamaso pake, koma Chauta amaweruza zamumtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:12

Samalani mayendedwe anu pakati pa akunja, kuti ngakhale azikusinjirirani kuti ndinu anthu ochita zoipa, komabe aziwona ntchito zanu zabwino. Apo adzalemekeza Mulungu pa tsiku limene Iye adzaŵayendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:8

Potsiriza, abale, muziika mtima pa zilizonse zabwino kwambiri ndi zotamandika, monga izi: zinthu zoona ndi zolemekezeka, zinthu zolungama, zoyera, zokongola, ndi zaulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:160

mau anu ndi oona okhaokha, malangizo anu onse olungama ngamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:8

Chachikulu nchakuti muzikondana mosafookera, popeza kuti chikondi chimaphimba machimo ochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:18

Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa, koma woyenda mokhotakhota adzagwa m'dzenje.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:17

Mu ufumu wa Mulungu chachikulu si chakudya kapena zakumwa ai, koma chilungamo, mtendere ndi chimwemwe, zimene Mzimu Woyera amapereka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 8:7

Pakamwa panga palankhula zoona, kulankhula zoipa nchinthu chonyansa m'kamwa mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
3 Yohane 1:4

Palibe chondikondweretsa kwambiri koposa kumva kuti ana anga akuyenda m'choona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:18

Ananu, chikondi chathu chisamangokhala cha nkhambakamwa chabe, koma chiziwoneka pa zochita zathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:19

Abale anga okondedwa, gwiritsani mau aŵa: munthu aliyense azifulumira kumva, koma kulankhula asamafulumira, ndipo kukwiya asamafulumiranso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 112:5

Munthu amene amakongoza mosafuna phindu, amene amayendetsa ntchito zake mwachilungamo, zinthu zimamuyendera bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:5

Mboni yokhulupirika siinama, koma mboni yonyenga imalankhula zabodza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:27

Munthu wofunafuna phindu monyenga amavutitsa banja lake, koma munthu wodana ndi ziphuphu adzapeza bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:16

Monga unenera Uthenga Wabwino umene ndimalalika, zidzateronso pa tsiku lija limene Mulungu mwa Khristu Yesu adzaweruza zinsinsi za m'mitima mwa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:9

Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, wolankhula mabodza adzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:17

Chakudya chochipeza monyenga chimamkomera munthu, koma pambuyo pake chimakasanduka ngati lubwe m'kamwa mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:14

Mfumu ikamaweruza osauka mosakondera, ufumu wake udzakhazikika mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:3

Kuchita zolungama ndi zokhulupirika kumakondweretsa Chauta koposa kupereka nsembe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:6

Tikanena kuti timayanjana naye, pamene tikuyendabe mu mdima, tikunama, ndipo zochita zathu nzosagwirizana ndi zoona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:1

“Chenjerani, musachite ntchito zanu zabwino pamaso pa anthu ndi cholinga choti akuwoneni. Mukatero, simudzalandira mphotho kwa Atate anu amene ali Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:6

Ndithudi, Inu mumakonda mtima woona, choncho mundiphunzitse nzeru zanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:13

Mayendedwe athu akhale oyenera, ngati a anthu oyenda usana. Pasakhale dyera kapena kuledzera, dama kapena zonyansa, ndeu kapena nsanje.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 101:6

Koma anthu okhulupirika am'dziko, ndidzaŵayang'ana moŵakomera mtima, ndipo adzakhala ndi ine. Oyenda m'njira yopanda cholakwa adzanditumikira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 13:6

Sichikondwerera zosalungama, koma chimakondwerera choona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:22

Musamadzinyenga pakungomva chabe mau a Mulungu, koma muzichita zimene mauwo anena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:1

Mbiri yabwino ndi yofunika kupambana chuma chambiri, kupeza kuyanja nkopambana siliva ndi golide.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:28

Munthu wabwino amaganizira za m'mene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woipa pamatuluka mau oipa okhaokha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:29

Mundichotse m'njira zondisokeza, kuti ndisayendemo. Mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:163

Ndimadana ndi anthu abodza, zoonadi, ndimanyansidwa nawo, koma ndimakonda malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:14

Mtima wa munthu womvetsa zinthu umafunitsitsa ndithu kudziŵa zambiri, koma m'kamwa mwa anthu opusa zauchitsiru zili pha!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:23

Tilimbikire kuvomereza mosafookera zimene timaziyembekeza, pakuti Iye amene adatilonjeza zimenezi ngwokhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:26

Munthu woyankha zoona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:33

Kuwopa Chauta kumaphunzitsa nzeru, ndipo ndi kudzichepetsa ndi ulemu, chili patsogolo nkudzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:2

Woyenda molungama amaopa Chauta, koma woyenda mokhotakhota amanyoza Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:22

Mwayeretsa mitima yanu pakumvera choona, kotero kuti muzikondana ndi akhristu anzanu mosanyenga. Nchifukwa chake muzikondana ndi mtima wonse, mosafookera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 24:16

Nchifukwa chake inenso ndimayesetsa nthaŵi zonse kukhala ndi mtima wangwiro pamaso pa Mulungu, ndi pamaso pa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:17

Wolankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yonama imalankhula monyenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 16:10

Wokhulupirika pa zinthu zazing'ono, ngwokhulupirikanso pa zazikulu. Ndipo wonyenga pa zazing'ono, amanyenganso pa zazikulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 27:4

pakamwa panga sipadzatuluka mau oipa, lilime langa silidzalankhula zonyenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:6

Munthu wosauka amene amayenda mwaungwiro amaposa kwambiri munthu wolemera amene ali wonyenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 112:4

Ngakhale nthaŵi ya mdima, munthu wochita chilungamo ayenda m'kuŵala, chifukwa ngwokoma mtima, wachifundo ndi woongoka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:30

Ine ndasankhula njira yoti ndizikhala wokhulupirika, ndaika malangizo anu mumtima mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 5:12

Koma koposa zonse abale anga, musamalumbira. Musalumbire potchula Kumwamba, kapena dziko lapansi, kapena china chilichonse. Pofuna kutsimikiza kanthu, muzingoti, “Inde”. Pofuna kukana kanthu, muzingoti, “Ai”. Muzitero, kuwopa kuti Mulungu angakuweruzeni kuti ndinu opalamula.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:10

Masikelo ndi miyeso ina yoyesera zinthu zikakhala zonyenga, zonsezo zimamunyansa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:8

Ngodala anthu oyera mtima, pakuti adzaona Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 8:15

Koma mbeu zogwera pa nthaka yabwino zija zikutanthauza anthu amene amaŵamva mau a Mulungu, naŵasunga mu mtima woona ndi wabwino, ndipo amalimbikira mpaka kubereka zipatso.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 141:3

Muike mlonda pakamwa panga, Inu Chauta. Mulonde pa khomo la milomo yanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:9

Musamauzana mabodza, pakuti mwachita ngati mwavula moyo wanu wakale, pamodzi ndi zochitachita zake zoipa,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 4:2

Takaniratu njira zonse zochititsa manyazi zimene anthu amatsata mobisika. Sitichita kanthu monyenga kapena kupotoza mau a Mulungu; koma pakulankhula zoona poyera pamaso pa Mulungu, tifuna kuti anthu onse ativomereze m'mitima mwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 19:11

“Musabe, musachite zinthu zonyenga, ndipo musaname.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:1

Wosauka amene amayenda molungama amaposa munthu wopusa wolankhula zokhota.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:5

Kudzudzula munthu poyera nkwabwino kupambana kubisa chikondi chimene uli nacho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:16

Kukwiya kwa munthu wopusa kumadziŵika msanga, koma munthu wanzeru salabadako za chipongwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:23

Miyeso yosintha imanyansa Chauta, masikelo onyenga ndi oipanso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:5

Munthu wokonda Mulungu amadana ndi bodza, koma zochita za munthu woipa zimanyansa ndipo zimachititsa manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 25:21

Kukhulupirika kwanga ndi kulungama kwanga kunditeteze, popeza kuti ndakukhulupirirani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:14

Imirirani tsono mutavala choona ngati lamba m'chiwuno mwanu. Valani chilungamo ngati chovala chachitsulo chotchinjirizira pachifuwa panu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:1

Muyeso wonyenga umanyansa Chauta, koma muyeso wachilungamo umamkondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:24

Ulekeretu kulankhula zokhotakhota, usiyiretu kukamba zopotoka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 101:7

Palibe munthu wochita zonyenga amene adzakhale m'nyumba mwanga. Palibe munthu wolankhula zabodza amene adzakhale pafupi ndi ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 8:16

Muzichita izi: muzikambirana zoona, muziweruza moona ndi mwamtendere m'mabwalo a milandu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:22

Pakamwa pabodza pamamnyansa Chauta. Koma anthu ochita zinthu mokhulupirika amamkondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 6:16-17

Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Chauta amadana nazo, makamaka zisanu ndi ziŵiri ndithu zimene zimamunyansa: maso onyada, pakamwa pabodza, manja opha munthu wosalakwa,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:3

Ungwiro wa anthu olungama umaŵatsogolera, koma makhalidwe okhota a anthu onyenga ngoononga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:6

Chuma chomachipeza monyenga chimangoti wuzi ngati nthunzi, ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:13

Mau oona amakondweretsa mfumu, ndipo imamkonda munthu wolankhula chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:25

Tsono lekani kunama. Aliyense azilankhula zoona zokhazokha ndi mkhristu mnzake, pakuti tonse pamodzi mogwirizana ndife ziwalo za thupi la Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 15:2

Ndi munthu amene amayenda mosalakwa, amene amachita zolungama nthaŵi zonse, amene amalankhula zinthu ndi mtima woona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:9

Munthu woyenda mwaungwiro, amayenda mosatekeseka. Koma woyenda njira zoipa, adzadziŵika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:13

Ngati ufunadi moyo, usalankhule zoipa, pakamwa pako pasakambe zonyenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:16

“Usachite umboni womnamizira mnzako.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 6:2

Kodi udakodwa ndi mau a pakamwa pako pomwe, kodi udagwidwa ndi mau olankhula iwe wemwe?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:19

Mau oona amakhala mpaka muyaya, koma zabodza sizikhalitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:4

Mau a Chauta ndi olungama, zochita zake zonse amazichita mokhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:21-22

koma zonse muziziyesa bwino, kuti muwonetsetse ngati nzoona. Musunge zimene zili zabwino, ndipo mupewe choipa cha mtundu uliwonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:37

Muzingoti, ‘Inde,’ kapena ‘Ai.’ Zimene muwonjezerepo nzochokera kwa Satana, Woipa uja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:11

Chuma chochipeza mofulumira chidzanka chitha pang'onopang'ono, koma chochipeza pang'onopang'ono chidzanka chichulukirachulukira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:5

Maganizo a munthu wabwino ngoongoka, koma malangizo a munthu woipa ngonyenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:37

Upenye munthu wopanda cholakwa ndi wolungama, ndipo udzapeza kuti munthu wamtendere ali ndi zidzukulu zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:7

Munthu abwino amakhala mwachilungamo, ndipo Mulungu amadalitsa ana amene amatsata njira yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 23:12

Pajatu aliyense wodzikuza adzamchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamkuza.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 26:1

Inu Chauta, onetsani kuti ine ndine wosalakwa, pakuti ndimachita zolungama, ndipo ndakhulupirira Inu mosakayika konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 3:17

Koma nzeru zochokera Kumwamba, poyamba nzangwiro, kuwonjeza apo nzamtendere, zofatsa ndi zomvera bwino. Ndi za chifundo chambiri, ndipo zipatso zake zabwino nzochuluka. Nzeruzo sizikondera kapena kuchita chiphamaso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:18

Muzitipempherera ifeyo, pakuti sitipeneka konse kuti tili ndi mtima wopanda kanthu koutsutsa, ndipo tatsimikiza kuchita zonse mwachilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 33:15

Angathe kutero ndi amene amachita zolungama ndi kulankhula zoona, amene amakana phindu lolipeza monyenga, amene amakutumula manja ake kuti angagwire chiphuphu, amene amatseka makutu kuti angamve mau opangana za kupha anzao, amene amatsinzina kuti angaone zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:9

Chikondi chizikhala chopanda chiphamaso. Muzidana ndi zoipa, nkumaika mtima pa kuchita zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 12:24

Muzingoopa Chauta, ndipo muzimtumikira mokhulupirika ndi mtima wanu wonse. Nthaŵi zonse muziganizira zazikulu zimene wakhala akukuchitirani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 59:4

Palibe amene amaimba mnzake mlandu molungama, palibe wopita ku bwalo lamilandu moona. Amadalira zopanda pake, amangonena mabodza. Amangolingalira zamphulupulu, nachitadi zoipa zimene akuganiza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:5

Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi ozama, ndi munthu wanzeru yekha angazitulutse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:31

Tsono, kaya mulikudya, kaya mulikumwa, kaya mukuchita chilichonse, muzichita zonse kuti mulemekeze Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:17

Munthu akakuchitani choipa, musamubwezere choipa. Yesani kuchita zimene anthu onse amaziwona kuti nzabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:10

Paja mau a Mulungu akuti. “Yemwe afuna kukondwera ndi moyo, ndi kuwona masiku abwino, aletse lilime lake kulankhula zoipa, ndiponso milomo yake kunena mabodza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 6:8

Iyai, Chauta adakuwonetsa kale, munthu iwe, chimene chili chabwino. Zimene akufuna kuti uzichita ndi izi: uzichita zolungama, uzikhala wachifundo, ndipo uziyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 25:5

Munditsogolere m'choona chanu ndi kundilangiza, pakuti Inu ndinu Mulungu Mpulumutsi wanga, ndimadalira Inu masiku onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:32

Anthu omvera Mulungu amadziŵa zoyenera kulankhula, koma pakamwa pa anthu oipa pamatuluka zosayenera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:21

Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amatsata zolungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 8:21

Ifetu tikufuna kuchita zabwino, osati pamaso pa Ambuye pokha, komanso pamaso pa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa