Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

110 Mauvesi a m'Baibulo Okhudza Kuperekedwa ndi Kusakhulana

Munthu wamkulu koposa onse amene anakhalapo padziko lino lapansi anakumana ndi chinyengo chachikulu. Iye amene anali ndi mtima woyera ndi wowona mtima, wopanda choipa chilichonse, anationetsa chikondi chake ngakhale ambiri anam’tembenukira. Yesu wa ku Nazarete anachitiridwa chinyengo ndi ambiri, kuphatikizapo ineyo ndi iweyo.

Komabe, chitsanzo chake chimatiphunzitsa kuti kukhululukira ndiye mankhwala a ululu wobwera chifukwa cha chinyengo. Kumasula moyo wako ku mkwiyo ndikutsata mapazi abwino a Yesu kudzakubweretsera mphotho ya Atate.

Bisala m’chikondi cha Yesu ndi nsembe yake pa mtanda, ndipo posachedwapa udzachira ndikumwetulira chifukwa cha m’bandakucha wako watsopano. Lolani Mulungu agwire ntchito mwa inu.


Luka 22:48

Koma Yesu adamufunsa kuti, “Yudasi, mongadi ukupereka Mwana wa Munthu kwa adani pakumumpsompsona?”

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:21

“Mbale azidzapereka mbale wake kuti aphedwe, bambo azidzapereka mwana wake. Ana adzaukira makolo ao, mpaka kuŵaphetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:56

Koma zonsezi zachitika kuti ziwonekedi zimene aneneri adalemba.” Pamenepo ophunzira ake onse aja adathaŵa, kumusiya yekha.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:28

Munthu woipa mtima amafalitsa mkangano, kazitape amadanitsa anthu okhala pa chibwenzibwenzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 55:12-14

Akadakhala mdani wanga wondinyozayo, ndikadatha kupirira. Akadakhala mdani wanga wondichita chipongweyo, ndikadangobisala basi.

Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa wozoloŵerana naye, ndi amene ukuchita zimenezi.

Tinkakambirana nkhani zokoma tili aŵiri, tinkapembedza limodzi m'Nyumba ya Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:19

Amene amanka nachita ugogodi, amaulula zinsinsi. Nchifukwa chake usamagwirizane naye wolankhula zopusayo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 41:9

Ngakhalenso bwenzi langa lapamtima amene ndinkamkhulupirira, amene ankadya nane pamodzi, wandiwukira.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:14-16

Pambuyo pake Yudasi Iskariote, mmodzi mwa ophunzira khumi ndi aŵiri aja, adapita kwa akulu a ansembe.

Adakaŵafunsa kuti, “Kodi mudzandipatsa chiyani ndikadzampereka Yesuyu kwa inu?” Iwo adamupatsa ndalama zasiliva makumi atatu.

Tsono kuyambira pomwepo iye adayamba kufunafuna mpata womuperekera kwa iwo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 12:6

Ngakhale abale ako ndi anansi ako nawonso amakuchita chiwembu, onsewo amvana pa zokuimba mlandu, usaŵakhulupirire, ngakhale alankhule nawe mau okoma.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 24:10

Pa nthaŵi imeneyo ambiri adzataya chikhulupiriro chao, azidzaperekana nkumadana.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 25:19

Kukhulupirira munthu wosakhulupirika pa nthaŵi yamavuto kuli ngati kudya ndi dzino loŵaŵa, kapena kuyenda ndi mwendo wothyoka.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 3:13

Ungovomera kulakwa kwako. Vomera kuti udaukira Chauta Mulungu wako, kuti udapembedza nao milungu yachilendo patsinde pa mitengo yogudira, ndiponso kuti sudamvere mau anga,’ ” akuterotu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Zefaniya 3:4

Aneneri ake anali achabechabe, anthu osakhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 10:33-34

Adati, “Tilitu pa ulendo wa ku Yerusalemu. Kumeneko Mwana wa Munthu akukaperekedwa kwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi a Malamulo. Iwo akamuweruza ndi kugamula kuti aphedwe. Ndipo akampereka kwa anthu akunja.

Amenewo akamchita chipongwe, akamthira malovu, akamkwapula nkumupha. Koma patapita masiku atatu, Iye adzauka.”

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 4:10

Paja Dema adandisiya chifukwa chokonda zapansipano, adapita ku Tesalonika. Kresike adapita ku Galatiya, ndipo Tito adapita ku Dalamatiya.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 2:13

Anthu anga achita machimo aŵiri: andisiya Ine kasupe wa madzi opatsa moyo, adzikumbira okha zitsime, zitsime zake zong'aluka, zosatha kusunga madzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 49:3-4

“Rubeni mwana wanga wachisamba, ndiwe nkhongono zanga, ndiwe mphatso yoyamba ya mphamvu zanga. Mwa ana anga onse, wopambana ndiwe pa ulemerero ndi mphamvu.

Lili kuvuma kwa Mamure m'dziko la Kanani. Abrahamu adaagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efuroni Muhiti, kuti pakhale manda.

Kumeneko ndiko kumene adaika Abrahamu pamodzi ndi Sara mkazi wake. Isaki pamodzi ndi mkazi wake Rebeka, adaŵaikanso komweko, ndipo Leya ndidamuika komwekonso.

Mundawo pamodzi ndi phangalo adagula kwa Ahiti.”

Tsono Yakobe atamaliza kulangiza ana ake, adabwezeranso mapazi ake m'bedi ndipo adamwalira.

Uli ngati chigumula cha madzi oopsa, koma sudzakhalanso wopambana, chifukwa chakuti sudaope kugona pa bedi la ine bambo wako. Udaloŵa m'bedi langa, nuliipitsa!

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 13:28-29

Tsono Abisalomu adalamula antchito ake kuti, “Muwonetsetse nthaŵi imene Aminoni akhale ataledzera ndi vinyo. Ndikakuuzani kuti, ‘Kanthani Aminoni!’ Pomwepo mumuphe. Musaope, nanga sindine ndakulamulani? Mulimbe mtima, ndipo muchite chamuna.”

Choncho atumiki a Abisalomu adamchita Aminoni monga momwe adaaŵalamulira Abisalomu. Zitatero, ana onse aamuna a mfumu adadzambatuka, aliyense adakwera pa bulu wake, nathaŵa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 55:20-21

Mnzanga adatambasula dzanja lake kuti amenye abwenzi ake, adaphwanya chipangano chake.

Mau ake anali osalala kupambana batala, komabe mumtima mwake munali zankhondo. Mau ake anali ofeŵa kupambana mafuta, komabe anali ndi malupanga osololasolola.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:4

Simoni, wa m'chipani chandale cha Azelote; ndiponso Yudasi Iskariote, amene pambuyo pake adapereka Yesu kwa adani ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 16:17-18

Ndikukupemphani abale, chenjera nawoni anthu amene amapatutsa anzao naŵachimwitsa. Iwo amaphunzitsa zosiyana ndi zimene inu mudaphunzira. Muziŵalewa,

pakuti anthu otere satumikira Khristu Ambuye athu, koma amangotumikira zilakolako zao basi. Ndi mau okoma ndi oshashalika amanyenga anthu a mitima yoona.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 109:5-8

Motero amandibwezera zoipa m'malo mwa zabwino, amandiwonetsa chidani m'malo mwa chikondi changa.

Sankhulani munthu woipa kuti aweruze mlandu wa wondiwukirayo, iye aimbidwe mlandu ndi munthu woneneza anzake.

Pomuweruza apezeke kuti ali ndi mlandu, mapemphero ake akhale ngati kupalamula.

Masiku ake akhale oŵerengeka, wina alandire udindo wake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 15:33

Musadzinyenge. “Paja kuyanjana ndi anthu ochimwa kumaononga khalidwe.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:5

Mboni yokhulupirika siinama, koma mboni yonyenga imalankhula zabodza.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 33:1

Tsoka kwa iwe woonongawe, iwe amene sadakuwononge. Tsoka iwe wonyengawe, amene wina aliyense sadakunyenge. Iwe ukadzaleka kuwononga, adzakuwononga, ukadzaleka kunyenga, adzakunyenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:11

Adani anga onse amandinyodola, anzanga omwe amandiyesa chinthu chonyansa. Anthu odziŵana nawo amandiyesa chinthu choopsa. Anthu ondiwona mu mseu amandithaŵa.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:7

Musadzinyenge, nkosatheka kupusitsa Mulungu. Zimene munthu amabzala, adzakolola zomwezo.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:23

Tilimbikire kuvomereza mosafookera zimene timaziyembekeza, pakuti Iye amene adatilonjeza zimenezi ngwokhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 27:6

Amene amakukonda, ngakhale akupweteke, chikondi chake chimakhalapobe, mdani wako ngakhale akumpsompsone, nkunyenga chabe kumeneko.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 3:1-5

Udziŵe kuti pa masiku otsiriza kudzafika nthaŵi ya zovuta.

Tsono iwe wakhala ukunditsatira m'zophunzitsa zanga, mayendedwe anga, cholinga changa, chikhulupiriro changa, kuleza mtima kwanga, chikondi changa, kupirira kwanga,

mazunzo anga, ndi masautso anga, monga amene adaandigwera ku Antiokeya, ku Ikonio ndi ku Listara. Ndidaazunzikadi koopsa! Koma Ambuye adandipulumutsa pa zonsezi.

Onse ofuna kukhala ndi moyo wolemekeza Mulungu mwa Khristu Yesu, adzazunzikadi,

m'menemo anthu ochimwa ndi onyenga, adzanka naipiraipira, ndipo azidzanyenga ena nkumanyengedwanso iwo omwe.

Koma iwe, limbika pa zimene waphunzira ndipo wadziŵa kuti nzoona, paja ukuŵadziŵa amene adakuphunzitsa.

Ukudziŵanso kuti kuyambira ukali mwana waŵazoloŵera Malembo Oyera, amene angathe kukupatsa nzeru zopulumukira pakukhulupirira Khristu Yesu.

Malembo Oyera onse ndi Mulungu amene adaŵalembetsa mochita ngati kuŵauzira, ndipo amathandiza pakuphunzitsa choona, pakutsutsa zolakwa, pakuwongola zokhota, ndi pakuphunzitsa anthu za kukhala olungama.

Motero Malembo amathandiza munthu wa Mulungu kukhala wokhoza kwenikweni, ndi wokonzekeratu kuchita ntchito yabwino iliyonse.

Anthu adzakhala odzikonda, okonda ndalama, onyada, odzikuza, onyoza Mulungu, osamvera anakubala ao, osayamika, ndi oipitsa zinthu za Mulungu.

Adzakhala opanda chifundo, osapepeseka, ndi osinjirira anzao. Adzakhala osadzigwira, aukali, odana ndi zabwino,

opereka anzao kwa adani ao. Adzakhala osaopa chilichonse, odzitukumula, okonda zosangalatsa m'malo mokonda Mulungu.

Adzasamala maonekedwe ake okha a chipembedzo, nkumakana mphamvu zake. Anthu otere uziŵalewa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 12:1-2

Thandizeni, Inu Chauta, palibenso munthu wosamala za Inu, okhulupirika sapezekanso pakati pa anthu.

Aliyense amangonamiza mnzake, amathyasika ndi pakamwa pake, amalankhula ndi mitima iŵiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 4:10

Aŵiriwo akagwa, wina adzautsa mnzake. Koma tsoka amene ali yekha: akagwa, ndiye kuti zavuta, chifukwa palibe wina womuutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 17:13-14

Dzambatukani, Inu Chauta, mukumane nawo ndi kuŵagonjetsa. Mundipulumutse ndi lupanga lanu kwa anthu oipawo.

Inu Chauta, ndi dzanja lanu mundilanditse kwa adani, kwa anthu amene moyo wao umangosamala zapansipano. Muŵalange ndi zoŵaŵa zimene mudaŵasungira. Nawonso ana awo akhale nazo zambiri, ndipo iwowo asiyireko ana aonso.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 9:4

“Aliyense achenjere ndi mnzake, asakhulupirire ngakhale mbale wake. Zoona, aliyense amafuna kulanda malo a mbale wake. Aliyense amachitira mnzake ugogodi.

Mutu    |  Mabaibulo
Hoseya 6:7

“Koma anthuwo adaphwanya chipangano changa monga adachitira Adamu. Potero, adandichitira zosakhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:158

Ndimanyansidwa ndikamayang'ana anthu osakhulupirika, chifukwa satsata malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 18:30

“Nchifukwa chake Ine Ambuye Chauta ndikuti, Aisraele inu, aliyense mwa inu ndidzamuweruza molingana ndi ntchito zake. Lapani, tembenukani mtima, kuti machimo anu asakuwonongeni.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:31-32

Pambuyo pake Yesu adaŵauza kuti, “Nonsenu mukhumudwa nane nkundisiya usiku uno. Paja Malembo akuti, ‘Ndidzapha mbusa, ndipo nkhosa za msambiwo zidzangoti balala.’

Koma ndikadzauka kwa akufa, ndidzatsogola ndine kupita ku Galileya.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 3:1

Inu Chauta, ndili ndi adani ochuluka, anthu ambiri akundiwukira.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 12:52-53

Kuyambira tsopano m'banja limodzi mudzakhala anthu asanu ogaŵikana, atatu adzakangana ndi aŵiri, ndipo aŵiri adzakangana ndi atatu.

Bambo adzakangana ndi mwana wake wamwamuna, mwana wamwamuna adzakangana ndi bambo wake. Mai adzakangana ndi mwana wake wamkazi, mwana wamkazi adzakangana ndi mai wake. Apongozi adzakangana ndi mkazi wa mwana wao, ndipo mkaziyo adzakangana ndi apongozi akewo.”

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 2:11-13

Koma pamene Petro adafika ku Antiokeya, ndidamtsutsa poyera, chifukwa adaapezeka wolakwadi.

Pakuti asanafike anthu ena amene Yakobe adaaŵatuma, iye ankadya pamodzi ndi abale osakhala Ayuda. Koma atafika iwowo, iye adayamba kudzipatula, osafuna kudya nawonso, chifukwa choopa anthu amene ankafuna kuti omwe sali Ayuda aumbalidwe.

Abale ena onse ochokera ku Chiyuda nawonso adayamba kuchita chiphamaso, kotero kuti ngakhale Barnabasi yemwe adaatengeka nacho chiphamaso chaocho.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 29:5

Munthu amene amathyasika mnzake amadzitchera msampha yekha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 55:6-8

Ndipo ndimati, “Ndikadakhala ndi mapiko onga a njiŵa, bwenzi nditauluka kupita kutali kukapuma.

Inde, ndikadathaŵira kutali ndi kukakhala ku chipululu.

“Ndikadafulumira kupeza pobisalira mphepo yaukali yamkunthoyi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 5:26-28

Paja mwa anthu anga muli ena achifwamba, amene amalalira anzao monga m'mene amachitira otchera mbalame. Amatcha misampha nakola anthu.

Nyumba zao nzodzaza ndi chuma chochipeza mwachinyengo, ngati chitatanga chodzaza ndi mbalame. Nchifukwa chake adasanduka otchuka ndi olemera.

Adanenepa nkukhala a matupi osalala. Ntchito zao zoipa nzopanda malire, saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye, kuti iyende bwino, ndipo sateteza amphaŵi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:1

Nchifukwa chake tayani choipa chonse, kunyenga konse, chiphamaso, kaduka ndi masinjiriro onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 26:4-5

Sindikhala pamodzi ndi anthu onyenga, sindiyenda ndi anthu achiphamaso.

Ndimadana ndi anthu ochita zoipa, sindikhala pamodzi ndi anthu oipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 24:12

Tsono popeza kuti zoipa zizidzachulukirachulukira, chikondi chizidzacheperachepera pakati pa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 6:10

Pajatu kukonda ndalama ndi gwero la zoipa zonse. Chifukwa cha kuika mtima pa ndalama anthu ena adasokera, adasiya njira ya chikhulupiriro, ndipo adadzitengera zoŵaŵitsa mitima.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 1:21

Taonanitu! Mzinda umene kale udaali wokhulupirika ndi wachilungamo, tsopano ukuchita zadama. Mzinda umene kale udaali ndi anthu aungwiro, tsopano wadzaza ndi anthu opha anzao.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 10:1

Ntchentche zakufa zimaika fungo loipa m'mafuta onunkhira bwino. Choncho kupusa kwapang'ono kumatha kuwononga nzeru ndi ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:150

Anthu ankhanza ondizunza akuyandikira. Iwo ali kutali ndi malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:6

Anthu ambiri amalankhula za kukhulupirika kwao, koma ndani angathe kumpeza munthu wokhulupirika kwenikweni?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 144:8

amene amalankhula zabodza, ndipo amalumbira zonama.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 33:31

Anthu anga amadzasonkhana kwa iwe nakhala pansi kuti amve zimene iweyo unene. Koma akazimva, sazitsata zimenezo. Zokamba zao zimaonetsa chikondi, m'menemo mitima yao imangokonda phindu chabe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:9

Wokhululukira cholakwa amafunafuna chikondi, koma wosunga nkhani kukhosi amapha chibwenzi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 10:12

Tsono amene akuganiza kuti waimirira molimba, achenjere kuti angagwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 55:23

Koma Inu Mulungu mudzaŵaponya adani anga m'dzenje lozama lachiwonongeko. Anthu okhetsa magazi ndi onyenga sadzafika ngakhale theka la masiku ao. Koma ine ndidzadalira Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:15

“Chenjera nawoni aneneri onyenga. Amadza kwa inu ali ndi maonekedwe ofatsa ngati nkhosa, koma m'kati mwao ndi mimbulu yolusa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:38-39

Ndithu ndikudziŵa mosakayika konse kuti palibe kanthu kangatilekanitse ndi chikondi chake. Ngakhale imfa kapena moyo, ngakhale angelo kapena olamulira, ngakhale zinthu zimene zilipo tsopano, kapena zimene zidzaoneke m'tsogolomo, kapena zamphamvu zina zilizonse,

ngakhale zakumwamba kapena zapansi, kapenanso kanthu kena kalikonse kolengedwa, sikangadzatilekanitse ndi chikondi cha Mulungu, chimene tili nacho mwa Khristu Yesu Ambuye athu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 3:12

Abale, mchenjere, kuti pasapezeke wina aliyense mwa inu wokhala ndi mtima woipa ndi wosakhulupirira, womlekanitsa ndi Mulungu wamoyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:113

Ndimadana nawo anthu apaŵiripaŵiri, koma ndimakonda mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:15

Koma ngati muyamba kulumana ndi kukadzulana, muchenjere kuti mungaonongane kotheratu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 27:10

Ngakhale bambo wanga ndi mai wanga andisiye ndekha, Inu Chauta mudzandisamala.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:20

Woyenda ndi anthu anzeru nayenso amakhala ndi nzeru, koma woyenda ndi zitsiru adzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 59:14-15

Kuweruza kolungama kwalekeka, ndipo kuchita zaungwiro kwaiŵalika. Zoona sizikupezekanso m'mabwalo a milandu, ndipo chilungamo sichikutha kupezeka kumeneko.

Zoona zikusoŵa kumeneko, ndipo wina aliyense akapanda kuchita nawo zoipa, amapeza mavuto.” Chauta adaziwona zimenezi ndipo zidamunyansa kuti palibe chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 5:8

Khalani odziletsa, khalani maso. Mdani wanu Satana amakhala akuyenda uku ndi uku ngati mkango wobangula, kufunafuna woti amudye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:28

Chauta amakonda chilungamo, sadzaŵasiya okha anthu ake okhulupirika. Iye adzawasunga mpaka muyaya, koma adzaononga ana a anthu oipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 6:13-14

“Pakuti onse, ang'onoang'ono ndi akuluakulu omwe, ali ndi khwinthi la phindu lopeza mwakuba. Aneneri pamodzi ndi ansembe ao, onsewo ndi onyenga.

Iwo amapoletsa mabala a anthu anga pamwamba pokha. Amangonena kuti, ‘Kuli mtendere, kuli mtendere,’ chonsecho kulibe konse mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 24:10-13

Pa nthaŵi imeneyo ambiri adzataya chikhulupiriro chao, azidzaperekana nkumadana.

Kudzaoneka aneneri onama ambiri, amene azidzasokeza anthu ambiri.

Tsono popeza kuti zoipa zizidzachulukirachulukira, chikondi chizidzacheperachepera pakati pa anthu.

Koma yemwe adzalimbikire mpaka potsiriza, ameneyo ndiye adzapulumuke.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:5

Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, wolankhula mabodza sadzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 62:4

Cholinga chao nchongofuna kumtsitsa pa malo ake aulemu. Amakonda kulankhula zonama. Amadalitsa ndi pakamwa pao, koma mumtima mwao amatemberera.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 22:47-48

Yesu akulankhula choncho, padabwera khamu la anthu. Amene ankaŵatsogolera anali Yudasi, mmodzi mwa ophunzira khumi ndi aŵiri aja. Iyeyu adadza pafupi ndi Yesu kuti amumpsompsone.

Koma Yesu adamufunsa kuti, “Yudasi, mongadi ukupereka Mwana wa Munthu kwa adani pakumumpsompsona?”

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:30

amasinjirira, ndipo amadana ndi Mulungu. Ndi achipongwe, odzikuza, ndi onyada. Amafunafuna njira zatsopano zochitira zoipa, samvera makolo ao.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:26-27

Pakuti tikamachimwirachimwira mwadala, kwina tikudziŵa choona, palibenso nsembe ina iliyonse ingaperekedwe chifukwa cha machimo athuwo.

Pamenepo chotitsalira si china ai, koma kumangodikira ndi mantha chiweruzo, ndiponso moto woopsa umene udzaononga otsutsana ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 3:1

Pansi pano chinthu chilichonse chili ndi nyengo yake ndi nthaŵi yake yomwe adaika Mulungu:

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 15:4

Ndi amene amanyoza munthu womkana Mulungu, koma amalemekeza anthu omvera Chauta. Ndi amene amachitadi zimene walonjeza, ngakhale zikhale zoŵaŵa chotani.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:1

Abale, wina akagwa m'tchimo lililonse, inu amene Mzimu Woyera amakutsogolerani, mumthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe ndi zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 109:3

Ponseponse amandilankhula mau achidani, amandinena popanda chifukwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 50:6

Ndidaperekera msana wanga kwa ondimenya, ndiponso masaya anga kwa ondimwetula ndevu. Sindidaŵabisire nkhope ondinyoza ndi ondithira malovu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:9

Chikondi chizikhala chopanda chiphamaso. Muzidana ndi zoipa, nkumaika mtima pa kuchita zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 26:24-26

Munthu wachidani pakamwa pake pamalankhula zabwino, pamene mumtima mwake muli zonyenga.

Woteroyo akamalankhula mokometsa mau, usamkhulupirire, pakuti mumtima mwake mwadzaza zoipa.

Ngakhale amabisa chidani mochenjera, kuipa kwakeko kudzaoneka poyera pakati pa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 101:5

Munthu wosinjirira mnzake kuseri ndidzamcheteketsa. Wooneka wonyada ndi wodzikuza sindidzamulekerera.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:25

Yudasi, amene pambuyo pake adapereka Yesu, adafunsa kuti, “Monga nkukhala ine, Aphunzitsi?” Yesu adamuyankha kuti, “Wanena wekha.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:17

Bwenzi lako ndiye amakukonda nthaŵi zonse, ndipo mbale wako adabadwira kuti azikuthandiza pa mavuto.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 18:30-32

“Nchifukwa chake Ine Ambuye Chauta ndikuti, Aisraele inu, aliyense mwa inu ndidzamuweruza molingana ndi ntchito zake. Lapani, tembenukani mtima, kuti machimo anu asakuwonongeni.

Tayani zoipa zanu zonse zakale zimene mudachimwira Ine. Mukhale ndi mtima watsopano ndi nzeru zatsopano. Nanga muferenji, inu anthu a ku Israele?

Sindikondwera nayo imfa ya munthu wina aliyense. Nchifukwa chake lapani, kuti mukhale ndi moyo. Ndikutero Ine Ambuye Chauta.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 94:20

Kodi angathe kugwirizana nanu olamulira oipa, amene amapotoza malamulo anu olungama?

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 6:4-6

Anthu amene adataya chikhulupiriro chao, nkosatheka kuŵatsitsimutsa kuti atembenuke mtima. Iwowo kale Mulungu adaaŵaunikira, adaalaŵako mphatso yochokera Kumwamba, nkulandira nao Mzimu Woyera.

Ndipo adazindikira kukoma kwa mau a Mulungu, ndi mphamvu za nthaŵi imene inalikudzafika.

Tsono akamkana Mulungu tsopano, akuchita ngati kumpachika iwo omwe Mwana wa Mulungu, ndi kumnyozetsa poyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:8-9

Kuthaŵira kwa Chauta nkwabwino kupambana kukhulupirira munthu.

Kuthaŵira kwa Chauta nkwabwino kupambana kukhulupirira mafumu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 54:17

Koma iwe palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke. Onse okuneneza udzaŵatsutsa. Ndimo adzapezera atumiki anga, ndipo ndidzaŵapambanitsa ndine,” akuterotu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:13

Amene amanka nachita ukazitape, amaulula zinsinsi. Koma wa mtima wokhulupirika, amasunga pakamwa pake.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 2:4

ngakhale kuti anthu ena adaafuna kuti iyeyu aumbalidwe ndithu. Anthu ameneŵa adaabwera modzizimbayitsa ngati abale athu. Iwowo adangodzaloŵa ngati azondi kuti adzaone ufulu wathu umene tili nawo mwa Khristu Yesu. Ankafuna kutisandutsa akapolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 41:5-6

Koma adani anga ondifunira zoipa, amati, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti, kuti aiŵalike?”

Amene amabwera kudzandiwona, ndi wosakhulupirika, mumtima mwake amaganiza zoipa za ine, ndipo akatuluka, amakaziwanditsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 12:4-5

“Ndikukuuzani inu, abwenzi anga, kuti musamaopa anthu. Iwo angathe kupha thupi lokha, koma pambuyo pake alibenso china choti angachitepo.

Choncho inunso khalani okonzeka, pakuti Mwana wa Munthu adzabwera pa nthaŵi imene simukuyembekeza.”

Pamenepo Petro adati, “Ambuye, kodi fanizoli mukuphera ife tokha, kapena mukuuza onse?”

Yesu adati, “Tsono kapitao wokhulupirika ndi wanzeru ndani, amene mbuye wake adzamuike kuti aziyang'anira onse a m'nyumba mwake, nkumaŵagaŵira chakudya chao pa nthaŵi yake?

Ngwodala wantchito ameneyo, ngati mbuye wake pofika adzampeza akuchitadi zimenezi.

Ndithu ndikunenetsa kuti adzamuika woyang'anira chuma chake chonse.

“Koma ngati ndi wantchito woipa, mumtima mwake azidzati, ‘Mbuye wanga akuchedwa kubwera.’ Ndiye adzayamba kumenya antchito anzake, amuna ndi akazi, ndiponso kumadya, kumamwa ndi kuledzera.

Tsono mbuye wake adzangoti mbwe mwadzidzidzi, pa tsiku limene iye sakumuyembekeza. Choncho adzamlanga koopsa, ndipo adzamtaya ku malo a anthu osakhulupirika.

“Wantchito amene akudziŵa zimene mbuye wake amafuna, koma osakonzekera kuzichita, adzamkwapula kwambiri.

Koma wantchito amene sadziŵa zimene mbuye wake amafuna, tsono nkumachita zoyenera kumlanga nazo, adzamkwapula pang'ono. Aliyense amene adalandira zambiri, adzayenera kubweza zambiri. Ndipo amene adamsungiza zambiri, adzamlamula kuti abweze zochuluka koposa.”

“Ndidabwera kudzaponya moto pa dziko lapansi, ndipo ndikadakonda utayaka kale.

Koma ndikuchenjezeni: amene muyenera kumuwopa ndi Mulungu. Iye atalanda moyo wa munthu, ali nazonso mphamvu za kumponya m'Gehena. Ndithu ndi ameneyo amene muzimuwopa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:37

Muzingoti, ‘Inde,’ kapena ‘Ai.’ Zimene muwonjezerepo nzochokera kwa Satana, Woipa uja.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:6

Chuma chomachipeza monyenga chimangoti wuzi ngati nthunzi, ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 73:3-4

Pakuti ndinkachita nsanje ndi anthu odzikuza, pamene ndidaona anthu oipa akulemera.

Iwowo samva kupweteka konse. Matupi ao ndi onenepa ndi athanzi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 4:1-2

Mzimu Woyera akunena momveka kuti pa masiku otsiriza anthu ena adzataya chikhulupiriro chao. Adzamvera mizimu yonyenga ndi zophunzitsa zochokera kwa mizimu yoipa.

Nchifukwa chake timagwira ntchito kolimba, ndipo timayesetsa kupambana, pakuti chiyembekezo chathu chili pa Mulungu wamoyo, amene ali Mpulumutsi wa anthu onse, makamaka okhulupirira Khristu.

Uzilamula ndi kuphunzitsa zimenezi.

Munthu asakupeputse poona kuti ndiwe wachinyamata, koma ukhale chitsanzo kwa akhristu onse pa mau, pa mayendedwe, pa chikondi, pa chikhulupiriro ndi pa kuyera mtima.

Mpaka pamene ndidzabwere, uchite khama kuŵerengera anthu mau a Mulungu, kuŵalalikira ndi kuŵaphunzitsa.

Usanyozere mphatso yaulere ija ili mwa iweyi, imene udailandira kudzera m'mau otchulidwa m'dzina la Mulungu, pamene gulu la akulu a Mpingo lidaakusanjika manja.

Ntchito zimenezi uzizichita mosamala ndi modzipereka, kuti anthu onse aone kuti moyo wako wautumiki ukukulirakulira.

Udziyang'anire bwino wekha, ndi kusamala zimene umaphunzitsa. Ulimbikire kutero, chifukwa pakuchita zimenezi udzadzipulumutsa iwe wemwe, ndiponso anthu amene amamva mau ako.

Zophunzitsa zimenezi nzochokera ku chinyengo cha anthu onama, amene mumtima mwao adalembedwa chizindikiro ndi chitsulo chamoto.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 7:20

Ndithudi, pa dziko lapansi palibe munthu amene amachita zabwino zokhazokha osachimwa konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:32

Munthu wonyoza malangizo amangodzinyoza yekha, koma wovomera kudzudzula amapindula nzeru yomvetsa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:36

mwakuti adani a munthu adzakhala a m'banja mwake omwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 94:21-23

Amagwirizana kuti aononge anthu osalakwa, nagamula kuti opanda mlandu aphedwe.

Koma Chauta wasanduka linga langa londiteteza, Mulungu ndiye thanthwe langa lothaŵirako.

Adzaŵalanga chifukwa cha machimo ao, adzaŵaononga chifukwa cha kuipa kwao, zoonadi, Chauta, Mulungu wathu, ndiye amene adzaŵafafanize.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 3:4

Mpang'ono pomwe. Koma anthu adziŵe kuti zimene Mulungu amalankhula nzoonadi, ngakhale kuti anthu onse ndi onama. Ndi monga Malembo akunenera kuti, “Inu Mulungu, anthu adziŵe kuti mumanena zoona mukamalankhula, adziŵe kuti mumapambana mukamazenga mlandu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:12

Paja mau a Mulungu ndi amoyo ndi ogwira ntchito mwamphamvu. Ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse. Amabaya mpaka molumikizirana mwa moyo ndi mzimu, ndiponso molumikizirana mfundo ndi mafuta a m'mafupa. Amaweruza ngakhale zimene anthu amalingalira ndi kulakalaka m'mitima mwao.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:20-21

kupembedza mafano, ufiti, chidani, kukangana, kaduka, kupsa mtima, kudzikonda, kusagwirizana, kuchita mipatuko,

dumbo, kuledzera, kudakwa pa maphwando achipembedzo, ndi zina zotere. Ndikukuchenjezani tsopano, monga ndidaachitanso kale, kuti anthu amene amachita zotere, sadzalandirako Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 59:2

Machimo anu adakulekanitsani ndi Mulungu wanu, ndipo Iye wakufulatirani chifukwa cha machimo anuwo. Choncho saamva zimene inu mumanena.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 54:5

Adzaŵabwezera adani anga zoipa. Aonongeni, Inu Ambuye, chifukwa cha kukhulupirika kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 6:16-19

Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Chauta amadana nazo, makamaka zisanu ndi ziŵiri ndithu zimene zimamunyansa:

maso onyada, pakamwa pabodza, manja opha munthu wosalakwa,

mtima wokonzekera kuchita zoipa, mapazi othamangira msangamsanga ku zoipa,

mboni yonama yolankhula mabodza, ndi munthu woutsa chidani pakati pa abale.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye, ndikukutamandani chifukwa ndinu Wolungama, Woyera, Woyenera kutamandidwa ndi kupembedzedwa konse. Ndinu Mulungu wanga, mtendere wanga pakati pa mkuntho, ndi thandizo langa lapafupi. Ambuye, m'dzina la Yesu, ndikubwera kwa inu pakati pa chisoni ichi chomwe ndikukumana nacho monga chipongwe. Ndithandizeni kukhululukira chifukwa ndikumva kuti mphamvu zanga zatha, koma ndikumvetsa kuti pano mphamvu zanu ziyamba kugwira ntchito. Atate, choyamba chiritsani maganizo anga ndi mtima wanga, musalole kuti mkwiyo ndi chisoni chomwe ndikumva chiwononge moyo wanga, kapena ubale womwe ndili nawo ndi inu. Zoonadi, kukhulupirika kwanu ndi chikondi chanu ndizosayerekezeka Mulungu, chikondi chenicheni chimachokera kwa inu ndipo kudzera mwa Mzimu Woyera wanu, chifukwa chake ndikupemphani mundidzaze ndi chikondi kwa munthu uyu yemwe ndi zochita ndi mawu ake anayesa kuwononga mtima wanga, muchitire chifundo, chifukwa mawu anu amati: «Ambiri adzakhumudwa, ndipo adzaperekedzana, ndipo adzadana.»  Dalitsani Ambuye, chifukwa mawu anu akhala pothawirapo panga ndipo chikondi chanu chilipo pamene ndikudutsa m’chipongwe ichi. Inu Yesu munaperekedwa, munayesedwa, munakanidwa, munanyozedwa ndi kunyozedwa chifukwa cha ine, kuti mulipire mtengo wa zoipa zanga, pa inu Ambuye munali mtendere wanga. Ndipangitseni kumvetsa kuti anthufe ndife ofooka ndi osasinthasintha, ndipo timakonda kulakwitsa kapena kuti ena atilakwitse. Yeretsani maganizo anga, mtima wanga ndi malingaliro omwe mdani anayesa kubzala mwa ine awachotse m'dzina la Yesu. M'dzina la Yesu, Ameni.