Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


107 Mauvesi a Mulungu Okhudza Mtanda

107 Mauvesi a Mulungu Okhudza Mtanda

Mtanda uwu ndi chizindikiro cha nsembe yaikulu ya Yesu yopulumutsa anthu. Ndi chikondi chachikulu chomwe sichinachitikepo. Ndi umboni wa chikhululukiro chomwe sitinayenerere. Ndi Mulungu wokonda mbadwo woipa ndi wauchimo mwachilendo.

Mtanda umatikumbutsa kuti, ngakhale pakati pa mavuto ndi zowawa, pali chiyembekezo chomwe chimatilimbitsa. Mu mtanda muli kuwala pakati pa mdima, ndi chitonthozo chochokera mu lonjezo la moyo wosatha.

Kuyang'ana mtanda kumatipangitsa kuti tidzipende tokha ndikudzifunsa za tanthauzo la zochita zathu. Kumatilimbikitsa kuganizira za chikondi cha Mulungu chosatha ndi kufunitsitsa kwake kutipatsa mwayi wachiwiri. Ndi kudzera mu mtanda momwe timapezera chikhululukiro ndi kubwezeretsedwa ubwenzi ndi Mlengi wathu.

Mtanda umatilimbikitsa kutsegula mitima yathu ndikupereka miyoyo yathu monga nsembe, monga momwe Yesu anachitira. Umatipangitsa kudzikana tokha ndikutsatira mapazi ake, kubweretsa uthenga wake wachikondi ndi chifundo padziko lapansi.

Kuganizira za mtanda kutitsogolere kukhala moyo wotsatira malamulo a Mulungu, kusonyeza chifundo, chikhululukiro, ndi chikondi kwa anansi athu. Pa sitepe iliyonse yomwe timaponda, tipeze mphamvu zonyamula mtanda wathu ndikutsatira njira ya Yesu, podziwa kuti chikondi chake chosasinthika chimatiyandikira nthawi zonse.




1 Akorinto 1:18

Pakuti mau a mtanda ali ndithu chinthu chopusa kwa iwo akutayika, koma kwa ife amene tilikupulumutsidwa ali mphamvu ya Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 14:27

Ndipo aliyense amene sasenza mtanda wake wa mwini yekha, ndi kudza pambuyo panga, sangathe kukhala wophunzira wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:24

Pomwepo Yesu anati kwa ophunzira ake, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikane yekha, natenge mtanda wake, nanditsate Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 3:18

Pakuti ambiri amayenda, za amene ndinakuuzani kawirikawiri, ndipo tsopanonso ndikuuzani ndi kulira, ali adani a mtanda wa Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:14

Koma kudzitamandira ine konsekonse, iai, koma mu mtanda wa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene mwa Iye dziko lapansi lapachikidwira ine, ndi ine ndapachikidwira dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 19:25

Koma pamtanda wa Yesu anaimirira amake, ndi mbale wa amake, Maria, mkazi wa Kleopa, ndi Maria wa Magadala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 19:17

ndipo anasenza mtanda yekha, natuluka kunka kumalo otchedwa Malo a Bade, amene atchedwa mu Chihebri, Gologota:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:27

Ndipo inunso muchita umboni, pakuti muli ndi Ine kuyambira chiyambi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 5:30

Mulungu wa makolo athu anaukitsa Yesu, amene munamupha inu, ndi kumpachika pamtengo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 27:32

Ndipo pakutuluka pao anapeza munthu wa ku Kirene, dzina lake Simoni, namkakamiza iye kuti anyamule mtanda wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:23

ameneyo, woperekedwa ndi uphungu woikidwa ndi kudziwiratu kwa Mulungu, inu mwampachika ndi kumupha ndi manja a anthu osaweruzika;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:8

ndipo popezedwa m'maonekedwe ngati munthu, anadzichepetsa yekha, nakhala womvera kufikira imfa, ndiyo imfa ya pamtanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:5

Koma Iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, natundudzidwa chifukwa cha mphulupulu zathu; chilango chotitengera ife mtendere chinamgwera Iye; ndipo ndi mikwingwirima yake ife tachiritsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:24

amene anasenza machimo athu mwini yekha m'thupi mwake pamtanda, kuti ife, titafa kumachimo, tikakhale ndi moyo kutsata chilungamo; ameneyo mikwingwirima yake munachiritsidwa nayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:8

Koma Mulungu atsimikiza kwa ife chikondi chake cha mwini yekha m'menemo, kuti pokhala ife chikhalire ochimwa, Khristu adatifera ife.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 2:14

adatha kutifafanizira cha pa ifecho cholembedwa m'zoikikazo, chimene chinali chotsutsana nafe: ndipo anachichotsera pakatipo, ndi kuchikhomera ichi pamtanda;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 3:16

Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wake wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira Iye asatayike, koma akhale nao moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:38

Ndipo iye amene satenga mtanda wake, natsata pambuyo panga, sayenera Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:20

Ndinapachikidwa ndi Khristu; koma ndili ndi moyo; wosatinso ine ai, koma Khristu ali ndi moyo mwa ine; koma moyo umene ndili nao tsopano m'thupi, ndili nao m'chikhulupiriro cha Mwana wa Mulungu, amene anandikonda, nadzipereka yekha chifukwa cha ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 9:23

Ndipo Iye ananena kwa onse, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikanize yekha, nanyamule mtanda wake tsiku ndi tsiku, nanditsate Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 2:2

Pakuti ndinatsimikiza mtima kuti ndisadziwe kanthu mwa inu, koma Yesu Khristu, ndi Iye wopachikidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 23:33

Ndipo pamene anafika kumalo dzina lake Bade, anampachika Iye pamtanda pomwepo, ndi ochita zoipa omwe, mmodzi kudzanja lamanja ndi wina kulamanzere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:17

Pakuti Khristu sananditume ine kubatiza, koma kulalikira Uthenga Wabwino, si mu nzeru ya mau, kuti mtanda wa Khristu ungayesedwe wopanda pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 19:19

Koma Pilato analemba lembo, naliika pamtanda. Koma panalembedwa, YESU MNAZARAYO, MFUMU YA AYUDA.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:24

Koma iwo a Khristu Yesu adapachika thupi, ndi zokhumba zake, ndi zilakolako zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:6

podziwa ichi, kuti umunthu wathu wakale unapachikidwa pamodzi ndi Iye, kuti thupilo la uchimo likaonongedwe, kuti ife tisakhalenso akapolo a uchimo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 23:26

Ndipo popita naye, anagwira munthu, Simoni wa ku Kirene, alikuchokera kuminda, namsenza iye mtanda aunyamule pambuyo pake pa Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 3:13

Khristu anatiombola ku temberero la chilamulo, atakhala temberero m'malo mwathu; pakuti kwalembedwa, Wotembereredwa aliyense wopachikidwa pamtengo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:24-26

Pomwepo Yesu anati kwa ophunzira ake, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikane yekha, natenge mtanda wake, nanditsate Ine. Pakuti iye amene afuna kupulumutsa moyo wake adzautaya: koma iye amene ataya moyo wake chifukwa cha Ine, adzaupeza. Pakuti munthu adzapindulanji, akalandira dziko lonse, nataya moyo wake? Kapena munthu adzaperekanji chosintha ndi moyo wake?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 19:30

Pamene Yesu tsono adalandira vinyo wosasayo anati, Kwatha; ndipo anawerama mutu, napereka mzimu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:16

ndi kuti akayanjanitse awiriwa ndi Mulungu, m'thupi limodzi mwa mtandawo, atapha nao udaniwo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:10

Umo muli chikondi, sikuti ife tinakonda Mulungu, koma kuti Iye anatikonda ife, ndipo anatuma Mwana wake akhale chiombolo chifukwa cha machimo athu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:20

mwa Iyenso kuyanjanitsa zinthu zonse kwa Iye mwini, atachita mtendere mwa mwazi wa mtanda wake; mwa Iyetu, kapena za padziko, kapena za mu Mwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:4

Zoonadi Iye ananyamula zowawa zathu, ndi kusenza zisoni zathu; koma ife tinamuyesa wokhomedwa, wokanthidwa ndi Mulungu, ndi wovutidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:2

Yesu, ameneyo, chifukwa cha chimwemwe choikidwacho pamaso pake, anapirira mtanda, nanyoza manyazi, nakhala padzanja lamanja la mpando wachifumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:18

Pakuti Khristunso adamva zowawa kamodzi, chifukwa cha machimo, wolungama m'malo mwa osalungama, kuti akatifikitse kwa Mulungu; wophedwatu m'thupi, koma wopatsidwa moyo mumzimu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 5:21

Ameneyo sanadziwe uchimo anamyesera uchimo m'malo mwathu; kuti ife tikhale chilungamo cha Mulungu mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 9:28

kotero Khristunso ataperekedwa nsembe kamodzi kukasenza machimo a ambiri, adzaonekera pa nthawi yachiwiri, wopanda uchimo, kwa iwo amene amlindirira, kufikira chipulumutso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 3:10

kuti ndimzindikire Iye, ndi mphamvu ya kuuka kwake, ndi chiyanjano cha zowawa zake, pofanizidwa ndi imfa yake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 8:34

Ndipo anadziitanira khamulo la anthu pamodzi ndi ophunzira ake, nati kwa iwo, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikanize yekha, nanyamule mtanda wake, nanditsate Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:3

Pakuti chimene chilamulo sichinathe kuchita, popeza chinafooka mwa thupi, Mulungu anatumiza Mwana wake wa Iye yekha m'chifanizo cha thupi la uchimo, ndi chifukwa cha uchimo, natsutsa uchimo m'thupi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:12

Chifukwa chake ndidzamgawira gawo ndi akulu; ndipo adzagawana ndi amphamvu zofunkha; pakuti Iye anathira moyo wake kuimfa; ndipo anawerengedwa pamodzi ndi olakwa; koma ananyamula machimo a ambiri, napembedzera olakwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 12:32

Ndipo Ine, m'mene ndikakwezedwa kudziko, ndidzakoka anthu onse kwa Ine ndekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:7

Tili ndi maomboledwe mwa mwazi wake, chikhululukiro cha zochimwa, monga mwa kulemera kwa chisomo chake,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 27:42

Anapulumutsa ena, sangathe kudzipulumutsa yekha. Ndiye mfumu ya Aisraele; atsike tsopano pamtandapo, ndipo tidzamkhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:32

Iye amene sanatimane Mwana wake wa Iye yekha, koma anampereka chifukwa cha ife tonse, adzalekeranji kutipatsanso ife zinthu zonse kwaulere pamodzi ndi Iye?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 24:7

ndi kunena, kuti, Mwana wa Munthu ayenera kuperekedwa m'manja a anthu ochimwa, ndi kupachikidwa pamtanda, ndi kuuka tsiku lachitatu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:23

koma ife tilalikira Khristu wopachikidwa, kwa Ayudatu chokhumudwitsa, ndi kwa amitundu chinthu chopusa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:25

amene Mulungu anamuika poyera akhale chotetezera mwa chikhulupiriro cha m'mwazi wake, kuti aonetse chilungamo chake, popeza Mulungu m'kulekerera kwake analekerera machimo ochitidwa kale lomwe;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:6

Yesu ananena naye, Ine ndine njira, ndi choonadi, ndi moyo. Palibe munthu adza kwa Atate, koma mwa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 23:46

Ndipo pamene Yesu anafuula ndi mau aakulu, anati, Atate, m'manja mwanu ndipereka mzimu wanga. Ndipo pakutero anapereka mzimu wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:3

Pakuti munafa, ndipo moyo wanu wabisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:16

Umo tizindikira chikondi, popeza Iyeyu anapereka moyo wake chifukwa cha ife; ndipo ife tiyenera kupereka moyo wathu chifukwa cha abale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:2

Nyamuliranani zothodwetsa, ndipo kotero mufitse chilamulo cha Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 10:9

kuti ngati udzavomereza m'kamwa mwako Yesu ndiye Ambuye, ndi kukhulupirira mumtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:10

Ndi chifuniro chimenecho tayeretsedwa mwa chopereka cha thupi la Yesu Khristu, kamodzi, kwatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 10:45

Pakuti ndithu, Mwana wa Munthu sanadze kutumikiridwa, koma kutumikira, ndi kupereka moyo wake dipo la kwa anthu ambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 2:11

Okhulupirika mauwa: Pakuti ngati tidamwalira ndi Iye, tidzakhalanso moyo ndi Iye:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:11

Koma ine, abale, ngati ndilalikiranso mdulidwe, ndizunzikanso bwanji? Pamenepo chikhumudwitso cha mtanda chidatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:3-4

Pakuti ndinapereka kwa inu poyamba, chimenenso ndinalandira, kuti Khristu anafera zoipa zathu, monga mwa malembo; Nanga ifenso tili m'moopsa bwanji nthawi zonse? Ndifa tsiku ndi tsiku, ndilumbira pa kudzitamandira kwa inu, abale, kumene ndili nako mwa Khristu Yesu, Ambuye wathu. Ngati ndinalimbana ndi zilombo ku Efeso monga mwa munthu, ndipindulanji? Ngati akufa saukitsidwa, tidye timwe pakuti mawa timwalira. Musanyengedwe; mayanjano oipa aipsa makhalidwe okoma. Ukani molungama, ndipo musachimwe; pakuti ena alibe chidziwitso cha Mulungu. Ndilankhula kunyaza inu. Koma wina adzati, Akufa aukitsidwa bwanji? Ndipo adza nalo thupi lotani? Wopusa iwe, chimene uchifesa wekha sichikhalitsidwanso chamoyo, ngati sichifa; ndipo chimene ufesa, sufesa thupi limene lidzakhala, koma mbeu yokha kapena ya tirigu kapena ya mtundu wina; koma Mulungu aipatsa thupi monga afuna; ndi kwa mbeu yonse thupi lakelake. Nyama yonse siili imodzimodzi; koma ina ndi ya anthu, ndi ina ndiyo nyama ya zoweta, ndi ina ndiyo nyama ya mbalame, ndi ina ya nsomba. ndi kuti anaikidwa; ndi kuti anaukitsidwa tsiku lachitatu, monga mwa malembo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:29

M'mawa mwake anaona Yesu alinkudza kwa iye, nanena, Onani Mwanawankhosa wa Mulungu amene achotsa tchimo lake la dziko lapansi!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 1:29

kuti kwapatsidwa kwa inu kwaufulu chifukwa cha Khristu, si kukhulupirira kwa Iye kokha, komatunso kumva zowawa chifukwa cha Iye,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 50:6

Ndinapereka msana wanga kwa omenya, ndi masaya anga kwa iwo amene anakudzula tsitsi langa; sindinabisire nkhope yanga manyazi ndi kulavulidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:9

Ndipo tsono popeza tinayesedwa olungama ndi mwazi wake, makamaka ndithu tidzapulumuka mkwiyo wa Mulungu mwa Iyeyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:18-19

podziwa kuti simunaomboledwa ndi zovunda, golide ndi siliva, kusiyana nao makhalidwe anu achabe ochokera kwa makolo anu: koma ndi mwazi wa mtengo wake wapatali monga wa mwanawankhosa wopanda chilema, ndi wopanda banga, ndiwo mwazi wa Khristu:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:13

Palibe munthu ali nacho chikondi choposa ichi, chakuti munthu ataya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 6:20

Pakuti munagulidwa ndi mtengo wake wapatali; chifukwa chake lemekezani Mulungu m'thupi lanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 13:4

pakuti anapachikidwa mu ufooko, koma ali ndi moyo mu mphamvu ya Mulungu. Pakuti ifenso tili ofooka mwa Iye, koma tidzakhala ndi moyo pamodzi ndi Iye, mu mphamvu ya Mulungu, ya kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:10

amene anafa m'malo mwathu, kuti, tingakhale tidikira, tingakhale tigona, tikakhale ndi moyo pamodzi ndi Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:19

Ndipo pokhala nacho, abale, chilimbikitso chakulowa m'malo opatulika, ndi mwazi wa Yesu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:13

Koma tsopano mwa Khristu Yesu inu amene munali kutali kale, anakusendezani mukhale pafupi m'mwazi wa Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 9:14

koposa kotani nanga mwazi wa Khristu amene anadzipereka yekha wopanda chilema kwa Mulungu mwa Mzimu wosatha, udzayeretsa chikumbumtima chanu kuchisiyanitsa ndi ntchito zakufa, kukatumikira Mulungu wamoyo?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 27:46

Ndipo poyandikira ora lachisanu ndi chinai, Yesu anafuula ndi mau aakulu, kunena, Eli, Eli, lama sabakitani? ndiko kunena kuti, Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji Ine?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 52:14

Monga ambiri anazizwa ndi iwe Israele, momwemo nkhope yake yaipitsidwa ndithu, kupambana munthu aliyense, ndi maonekedwe ake kupambana ana a anthu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 5:15

ndipo adafera onse kuti iwo akukhala ndi moyo asakhalenso ndi moyo kwa iwo okha, koma mwa Iye amene adawafera iwo, nauka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 1:4

amene anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu, kuti akatilanditse ife m'nyengo ya pansi pano ino yoipa, monga mwa chifuniro cha Mulungu ndi Atate wathu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:28

pakuti ichi ndi mwazi wanga wa pangano wothiridwa chifukwa cha anthu ambiri ku kuchotsa machimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:42

nati, Atate, mukafuna Inu, chotsani chikho ichi pa Ine; koma si kufuna kwanga ai, komatu kwanu kuchitike.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 2:15

atavula maukulu ndi maulamuliro, anawaonetsera poyera, nawagonjetsera nako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 2:6

amene anadzipereka yekha chiombolo m'malo mwa onse; umboni m'nyengo zake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:3

Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu; munthu wazisoni, ndi wodziwa zowawa; ndipo ananyozedwa monga munthu wombisira anthu nkhope zao; ndipo ife sitinamlemekeze.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:15

Pakuti sitili naye mkulu wa ansembe wosatha kumva chifundo ndi zofooka zathu; koma wayesedwa m'zonse monga momwe ife, koma wopanda uchimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:10

Pakuti pakufa Iye, atafa ku uchimo kamodzi; ndipo pakukhala Iye wamoyo, akhala wamoyo kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 20:28

monga Mwana wa Munthu sanadze kutumikiridwa koma kutumikira, ndi kupereka moyo wake dipo la anthu ambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 1:5

ndi kwa Yesu Khristu, mboni yokhulupirikayo, wobadwa woyamba wa akufa, ndi mkulu wa mafumu a dziko lapansi. Kwa Iye amene atikonda ife, natimasula kumachimo athu ndi mwazi wake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:2

ndipo yendani m'chikondi monganso Khristu anakukondani inu, nadzipereka yekha m'malo mwathu, chopereka ndi nsembe kwa Mulungu, ikhale fungo lonunkhira bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:2

ndipo Iye ndiye chiombolo cha machimo athu; koma wosati athu okha, komanso a dziko lonse lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 22:16

Pakuti andizinga agalu, msonkhano wa oipa wanditsekereza; andiboola m'manja anga ndi m'mapazi anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 12:10

Ndipo ndidzatsanulira pa nyumba ya Davide, ndi pa okhala mu Yerusalemu, mzimu wa chisomo ndi wakupembedza; ndipo adzandipenyera Ine amene anandipyoza; nadzamlira ngati munthu alira mwana wake mmodzi yekha, nadzammvera zowawa mtima, monga munthu amvera zowawa mtima mwana wake woyamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:9

Mwa ichinso Mulungu anamkwezetsa Iye, nampatsa dzina limene liposa maina onse,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 2:9

Koma timpenya Iye amene adamchepsa pang'ono ndi angelo, ndiye Yesu, chifukwa cha zowawa za imfa, wovala korona wa ulemerero ndi ulemu, kuti ndi chisomo cha Mulungu alawe imfa m'malo mwa munthu aliyense.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 4:25

amene anaperekedwa chifukwa cha zolakwa zathu, naukitsidwa chifukwa cha kutiyesa ife olungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 3:1

Agalatiya opusa inu, anakulodzani ndani, inu amene Yesu Khristu anaonetsedwa pamaso panu, wopachikidwa?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 23:34

Ndipo Yesu ananena, Atate, muwakhululukire iwo, pakuti sadziwa chimene achita. Ndipo anagawana zovala zake, poyesa maere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 11:24-25

ndipo m'mene adayamika, ananyema, nati, Ichi ndi thupi langa la kwa inu; chitani ichi chikhale chikumbukiro changa. Koteronso chikho, chitatha chakudya, ndi kuti, Chikho ichi ndi pangano latsopano m'mwazi wanga; chitani ichi, nthawi zonse mukamwa, chikhale chikumbukiro changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 9:6

Pakuti kwa ife mwana wakhanda wabadwa, kwa ife mwana wamwamuna wapatsidwa; ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake, ndipo adzamutcha dzina lake Wodabwitsa, Wauphungu, Mulungu wamphamvu, Atate Wosatha, Kalonga wa mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 8:9

Pakuti mudziwa chisomo cha Ambuye wathu Yesu Khristu, kuti, chifukwa cha inu anakhala wosauka, angakhale anali wolemera, kuti inu ndi kusauka kwake mukakhale olemera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:39

Ndipo anamuka patsogolo pang'ono, nagwa nkhope yake pansi, napemphera, nati, Atate ngati nkutheka, chikho ichi chindipitirire Ine; koma si monga ndifuna Ine, koma Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:1

Popeza tsono tayesedwa olungama ndi chikhulupiriro, tikhala ndi mtendere ndi Mulungu mwa Ambuye wathu Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 22:1

Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine? Mukhaliranji kutali kwa chipulumutso changa, ndi kwa mau a kubuula kwanga?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:4

monga anatisankha ife mwa Iye, lisanakhazikike dziko lapansi, tikhale ife oyera mtima, ndi opanda chilema pamaso pake m'chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 27:54

Ndipo anali naye akudikira Yesu, anaona chivomezi, ndi zinthu zimene zinachitidwa, anaopa kwambiri, nanena, Indedi Uyu ndiye Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:1

Chifukwa chake tsopano iwo akukhala mwa Khristu Yesu alibe kutsutsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:21

Sindichiyesa chopanda pake chisomo cha Mulungu; pakuti ngati chilungamo chili mwa lamulo, Khristu adafa chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:22

koma tsopano anakuyanjanitsani m'thupi lake mwa imfayo, kukaimika inu oyera, ndi opanda chilema ndi osatsutsika pamaso pake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:44

Ndipo pokhala Iye m'chipsinjo mtima anapemphera kolimba koposa ndithu: ndi thukuta lake linakhala ngati madontho aakulu a mwazi alinkugwa pansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 7:27

amene alibe chifukwa cha kupereka nsembe tsiku ndi tsiku monga akulu a ansembe, yoyambira chifukwa cha zoipa za iwo eni, yinayi chifukwa cha zoipa za anthu; pakuti ichi anachita kamodzi, kwatha, podzipereka yekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Zikomo Ambuye Atate wanga wakumwamba, ine wochimwa munatumiza Mwana wanu Yesu kuti adzafere machimo anga. Zikomo chifukwa cha chisomo chanu chimene simunayenera, koma ngakhale kuipa kwanga konse, magazi a Yesu ndi amphamvu kuti anditsuke ndi kuchotsa kupanduka kwanga. Zikomo Yesu chifukwa pa mtanda munatenga ululu wanga wonse, munatenga matenda anga, munavutika zonse zomwe zinandiyenera ine kuti ndikhale ndi ufulu wonse. Pa mtanda pomwepo munaletsa chikalata cha milandu yomwe inandidzudzula, ndipo munalembera ine nkhani yatsopano. Ndingakulephereni bwanji kukulambirani, ndingakulephereni bwanji kukutumikirani ndi moyo wanga wonse, popeza inu munapereka zonse chifukwa cha ine? Tsiku lililonse ndikufuna kutenga mtanda wanu ndikuyenda m'chifuniro chanu, ndikuchita zonse zomwe munabwerera padziko lapansi ndikundikonda. Ndidzipereka kwa inu, ndikufuna kukhala wanu kwathunthu ndi kupereka zonse chifukwa cha inu Yesu, chifukwa ndinu woyamba ndipo mukuyenera zonse zomwe ndili. Mutamandike muyambe muyambe kwamuyaya. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa