Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 22:16 - Buku Lopatulika

16 Pakuti andizinga agalu, msonkhano wa oipa wanditsekereza; andiboola m'manja anga ndi m'mapazi anga.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

16 Pakuti andizinga agalu, msonkhano wa oipa wanditsekereza; andiboola m'manja anga ndi m'mapazi anga.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

16 Anthu ankhanza andizinga ngati mimbulu. Aboola manja anga ndi mapazi anga.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

16 Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 22:16
27 Mawu Ofanana  

Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine? Mukhaliranji kutali kwa chipulumutso changa, ndi kwa mau a kubuula kwanga?


Landitsani moyo wanga kulupanga; wokondedwa wanga kumphamvu ya galu,


Ondikonda ndi anzanga apewa mliri wanga; ndipo anansi anga aima patali.


Ndipo abwere madzulo, auwe ngati galu, nazungulire mzinda.


Abwera madzulo, auwa ngati galu, nazungulira mzinda.


Mulungu, odzikuza andiukira, ndi msonkhano wa anthu oopsa afuna moyo wanga, ndipo sanaike Inu pamaso pao.


Koma Iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, natundudzidwa chifukwa cha mphulupulu zathu; chilango chotitengera ife mtendere chinamgwera Iye; ndipo ndi mikwingwirima yake ife tachiritsidwa.


Pakuti ngakhale abale ako, ndi nyumba ya atate wako, ngakhale iwo anakunyenga iwe; ngakhale anakufuulira iwe; usamvere iwo, ngakhale anena nawe mau abwino.


Ndipo ndidzatsanulira pa nyumba ya Davide, ndi pa okhala mu Yerusalemu, mzimu wa chisomo ndi wakupembedza; ndipo adzandipenyera Ine amene anandipyoza; nadzamlira ngati munthu alira mwana wake mmodzi yekha, nadzammvera zowawa mtima, monga munthu amvera zowawa mtima mwana wake woyamba.


Ndipo iwo akugwira Yesu ananka naye kwa Kayafa, mkulu wa ansembe, kumene adasonkhana alembi ndi akulu omwe.


Ndipo pamene anampachika Iye, anagawana zovala zake ndi kulota maere:


Musamapatsa chopatulikacho kwa agalu, ndipo musamaponya ngale zanu patsogolo pa nkhumba, kuti zingazipondereze ndi mapazi ao, ndi potembenuka zingang'ambe inu.


Ndipo anampachika Iye, nagawana zovala zake mwa iwo okha, ndi kuchita maere pa izo, kuti adziwe yense adzatenga chiyani.


Koma anakakamiza ndi mau okweza, napempha kuti Iye apachikidwe. Ndipo mau ao anapambana.


Ndipo pamene anafika kumalo dzina lake Bade, anampachika Iye pamtanda pomwepo, ndi ochita zoipa omwe, mmodzi kudzanja lamanja ndi wina kulamanzere.


Pamenepo asilikali, m'mene adapachika Yesu, anatenga zovala zake, anadula panai, natenga wina china, wina china, ndiponso malaya; koma malaya anaombedwa monsemo kuyambira pamwamba pake, analibe msoko.


koma mmodzi wa asilikali anamgwaza ndi nthungo m'nthiti yake, ndipo panatuluka pomwepo mwazi ndi madzi.


Ndipo linenanso lembo lina, Adzayang'ana pa Iye amene anampyoza.


Chifukwa chake ophunzira ena ananena naye, Tamuona Ambuye. Koma iye anati kwa iwo, Ndikapanda kuona m'manja ake chizindikiro cha misomaliyo, ndi kuika chala changa m'chizindikiro cha misomaliyo, ndi kuika dzanja langa kunthiti yake; sindidzakhulupirira.


Pomwepo ananena kwa Tomasi, Bwera nacho chala chako kuno, nuone manja anga, ndipo bwera nalo dzanja lako, nuliike kunthiti yanga, ndipo usakhale wosakhulupirira, koma wokhulupirira.


Penyererani agalu, penyererani ochita zoipa, penyererani choduladula;


Kunja kuli agalu ndi anyanga, ndi achigololo, ndi ambanda, ndi opembedza mafano, ndi yense wakukonda bodza ndi kulichita.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa