Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 22:15 - Buku Lopatulika

15 Mphamvu yanga yauma ngati phale; ndi lilime langa likangamira kunsaya zanga; ndipo mwandifikitsa kufumbi la imfa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

15 Mphamvu yanga yauma ngati phale; ndi lilime langa likangamira kunsaya zanga; ndipo mwandifikitsa kufumbi la imfa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

15 Kukhosi kwanga kwauma ngati phale, lilime langa lakangamira ku nsagwada. Inu mwandisiya pa fumbi kuti ndifere pomwepo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

15 Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 22:15
22 Mawu Ofanana  

Ndipo anayankha Abrahamu nati, Taonanitu, ndadziyesera kunena kwa Ambuye, ine ndine fumbi ndi phulusa:


m'thukuta la nkhope yako udzadya chakudya, kufikira kuti udzabwerera kunthaka: chifukwa kuti m'menemo unatengedwa: chifukwa kuti ndiwe fumbi, ndi kufumbiko udzabwerera.


Pakuti kufa tidzafa, ndipo tili ngati madzi otayika pansi amene sangathe kuwaolanso; ngakhale Mulungu sachotsa moyo, koma alingalira njira yakuti wotayikayo asakhale womtayikira Iye.


Mukumbukire kuti mwandiumba ngati dothi; ndipo kodi mudzandibwezera kufumbi?


Fupa langa laumirira pa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo ndapulumuka ndili nazo nkhama za mano anga.


mau a omveka anali zii, ndi lilime lao linamamatira kumalakalaka ao.


Ndipo tsopano moyo wanga udzitsanulira m'kati mwanga; masiku akuzunza andigwira.


zamoyo zonse zidzatsirizika pamodzi, ndi munthu adzabwerera kufumbi.


Mulekeranji kukhululukira kulakwa kwanga ndi kundichotsera mphulupulu yanga? Popeza tsopano ndidzagona kufumbi; mudzandifunafuna, koma ine palibe.


Mukabisa nkhope yanu, ziopsedwa; mukalanda mpweya wao, zikufa, ndipo zibwerera kufumbi kwao.


M'mwazi mwanga muli phindu lanji, potsikira ine kudzenje? Ngati fumbi lidzayamika Inu? Ngati lidzalalikira choonadi chanu?


Mtima wanga ugundagunda, mphamvu yanga yachoka, ndipo kuunika kwa maso anga, ndi iko komwe kwandichokera.


Ndipo anandipatsa ndulu ikhale chakudya changa; nandimwetsa vinyo wosasa pomva ludzu ine.


Ndalema ndi kufuula kwanga; kum'mero kwauma gwaa! M'maso mwanga mwada poyembekeza Mulungu wanga.


Mtima wosekerera uchiritsa bwino; koma mzimu wosweka uphwetsa mafupa.


Chifukwa chake ndidzamgawira gawo ndi akulu; ndipo adzagawana ndi amphamvu zofunkha; pakuti Iye anathira moyo wake kuimfa; ndipo anawerengedwa pamodzi ndi olakwa; koma ananyamula machimo a ambiri, napembedzera olakwa.


Lilime la mwana woyamwa limamatira kumalakalaka kwake ndi ludzu; ana aang'ono apempha mkate koma palibe wakuwanyemera.


Ndipo ambiri a iwo ogona m'fumbi lapansi adzauka, ena kunka kumoyo wosatha, ndi ena kumanyazi ndi mnyozo wosatha.


Ndipo Yesu, pamene anafuula ndi mau aakulu, anapereka mzimu wake.


Chitapita ichi Yesu, podziwa kuti zonse zidatha pomwepo kuti lembo likwaniridwe, ananena, Ndimva ludzu.


Pakuti ndinapereka kwa inu poyamba, chimenenso ndinalandira, kuti Khristu anafera zoipa zathu, monga mwa malembo;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa