Ambiri aife timathera nthawi yambiri tikusamalira maonekedwe athu akunja, tifuna kuoneka okongola, koma timanyalanyaza mkati mwathu. Pakati pa kudzikuza ndi moyo wothamanga, anthu ambiri amatanganidwa ndi zovala zamakono, koma aiwala zofunika kwambiri: mkati mwawo.
Baibulo, mu Aefeso 4:24, limati: “Muvale umunthu watsopano, wolengedwa m’chifanizo cha Mulungu mu chilungamo chenicheni ndi chiyero.” Mulungu sakonda kuti uzikongoletsa thupi lako lokha, koma mzimu wako ukhale wauve. Sakufuna kuti uvale zinthu zosayera ndi zosayenera.
Pakali pano, Mzimu Woyera akukuitanira kuti uvale chiyero. Pamene walandira Yesu mumtima mwako, uyenera kuyesetsa kwambiri kusunga chipulumutso chako kudzera mu chiyero, chifukwa popanda chiyero sungamuone Yesu.
Taya chilichonse chodetsa mzimu wako, chilichonse choipa, chilichonse chomwe chimakhumudwitsa Mzimu Woyera ndikukulekanitsa ndi Iye. Mulungu sakufuna kuti moyo wako utaike. Konza moyo wako ndi Yesu tsopano, ndipo chovala chako chabwino kwambiri chikhale chiyero.
Kudzikongoletsa kwanu kusangokhala kwa maonekedwe akunja pakuluka tsitsi, ndi kuvala zamakaka zagolide ndi zovala zamtengowapatali.
Koma kudzikongoletsa kwanu kukhale kwa moyo wam'kati, kukongola kosatha kwa mtima wofatsa ndi wachete. Moyo wotere ngwamtengowapatali pamaso pa Mulungu.
Popeza kuti mudasankhidwa ndi Mulungu kuti mukhale akeake, ndipo Iye amakukondani, muzikhala a mtima wachifundo, okoma mtima, odzichepetsa, ofatsa ndi odziŵa kupirira.
Ndipo muvale moyo watsopano, umene Mulungu adaulenga, wofanafana naye. Apo mudzakhala olungama ndi oyera mtima kwenikweni.
Motero aliyense amene adzapambane, adzamuvekanso zovala zoyera. Dzina lake sindidzalifafaniza m'buku la amoyo, ndipo ndidzamchitira umboni pamaso pa Atate anga, ndi pamaso pa angelo ao.
Tsono ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Chauta, mtima wanga ukukondwadi chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso. Wandiveka mkanjo wa chilungamo. Zinali ngati mkwati wamwamuna wavala nkhata ya maluŵa m'khosi, ndiponso ngati mkwati wamkazi wavala mikanda ya mtengo wapatali.
Zovala zimene udzasokezo ndi izi: chovala chapachifuwa, chovala cha efodi, mkanjo, mwinjiro wopetedwa bwino, nduŵira ndi lamba. Asoke zovala zopatulikazo za mbale wako Aroni ndi za ana ake, kuti akhale ansembe onditumikira.
“Ndipo mumaderanji nkhaŵa ndi zovala? Onani maluŵa akuthengo m'mene amakulira. Sagwira ntchito kapena kuwomba nsalu ai.
Komatu kunena zoona, ngakhale mfumu Solomoni yemwe, mu ulemerero wake wonse, sankavala zokongola kulingana ndi limodzi lomwe mwa maluŵa ameneŵa.
Koma iwe ukamapereka zachifundo, dzanja lako lamanzere lisadziŵe zimene dzanja lako lamanja likuchita.
Tsono ngati Mulungu amaveka motere udzu wakuthengo, umene ungokhalapo lero lokha, maŵa lino nkuponyedwa pa moto, nanji inuyo, angapande kukuvekani, inu a chikhulupiriro chochepanu?
Pajatu nonsenu amene mudasanduka amodzi ndi Khristu pakubatizidwa, mudachita ngati kuvala moyo wa Khristu.
Mukatenga mwinjiro wa munthu wina ngati chigwiriro kuti adzakulipireni, muubweze dzuŵa lisanaloŵe,
poti chofunda nchokhacho, ndicho chotetezera thupi lake. Nanga adzafunda chiyani? Akalira kwa Ine iyeyu kuti ndimthandize, ndidzamuyankha chifukwa ndine wachifundo.
“Muzitsata malamulo anga. Musalole kuti ng'ombe zanu zikwerane ndi zoŵeta za mtundu wina. Musafese mbeu za mitundu iŵiri m'munda mwanu, ndipo musavale chovala chopangidwa ndi nsalu za mitundu iŵiri.
Ambuye Yesu Khristu mwini akhale chida chanu chankhondo. Lekani mtima wofunafuna zosangalatsa thupi, musagonjere zilakolako zake zoipa.
Tamanda Chauta, iwe mtima wanga. Inu Chauta, Mulungu wanga, ndinu aakulu kwambiri. Mumavala ulemu ndi ufumu.
Inu mumatumphutsa akasupe m'zigwa, mitsinje imayenda pakati pa mapiri.
Imapatsa nyama zonse zakuthengo madzi akumwa, mbidzi zimapherapo ludzu.
Mbalame zimamanga zisa pafupi ndi mitsinjeyo, zimaimba m'nthambi za mitengo.
Inu mumathirira mapiri ndi madzi ochokera ku malo anu akumwamba. Dziko lapansi ladzaza ndi madalitso anu.
Mumameretsa udzu kuti ng'ombe zidye, ndi zomera kuti munthu azilima ndi kupeza chakudya m'nthaka.
Amapezamo vinyo wosangalatsa mtima wake, mafuta odzola kuti thupi lake lisisire, ndiponso buledi kuti ampatse mphamvu.
Mitengo ya Chauta amaithirira ndi madzi ambiri, mikungudza ya ku Lebanoni imene adaibzala.
Mbalame zimamanga zisa m'menemo, dokowe amamanga chisa m'mikungudzamo.
M'mapiri aatali ndimo m'mene mumakhala mbalale, m'matanthwe ndimo m'mene mumathaŵira mbira.
Inu mudapanga mwezi kuti uzisiyanitsa nyengo, ndipo dzuŵa limadziŵa nthaŵi yake yoloŵera.
Mumadzifunditsa ndi kuŵala ngati chovala, mwatambasula mlengalenga ngati hema.
Munthu sati akayatsa nyale, nkuivundikira ndi mbiya. Koma amaiika pa malo oonekera, ndipo imaunikira anthu onse amene ali m'nyumbamo.
koma kuti kwa mkazi nchaulemu? Mulungu adapatsa mkazi tsitsi lalitali loti aziphimbira mutu wake.
Ansembe ake ndidzaŵaveka chipulumutso, anthu ake oyera mtima adzafuula ndi chimwemwe.
Azivala mwinjiro woyera wabafuta, azivalanso kabudula wabafuta ndi kumangira lamba wabafuta, ndipo avalenso nduŵira yabafuta kumutu. Zimenezi ndi zovala zopatulika. Avale zimenezi atasamba thupi lonse.
Abale anga, popeza kuti mumakhulupirira Ambuye athu Yesu Khristu, Ambuye aulemerero, musamakondera.
Pajatu munthu wotsata Malamulo onse, akangophonyapo ngakhale pa mfundo imodzi yokha, ndiye kuti wachimwira Malamulo onsewo.
Pakuti Mulungu amene adanena kuti, “Usachite chigololo”, adanenanso kuti, “Usaphe”. Ngati inu chigololo simuchita, koma kupha mumapha, ndiye kutitu mwachimwira Malamulo onse.
Tsono muzilankhula ndi kuchita zinthu monga anthu oti Mulungu adzaŵaweruza potsata lamulo loŵapatsa ufulu.
Paja munthu woweruza mopanda chifundo, nayenso Mulungu adzamuweruza mopanda chifundo. Koma wochita chifundo alibe chifukwa choopera chiweruzo cha Mulungu.
Abale anga, pali phindu lanji, ngati munthu anena kuti, “Ndili ndi chikhulupiriro,” koma popanda chimene akuchitapo? Kodi chikhulupiriro chotere chingampulumutse?
Mwachitsanzo: mbale wina kapena mlongo ali ndi usiŵa, ndipo masiku onse alibe chakudya chokwanira.
Tsono wina mwa inu angoŵauza kuti. “Pitani ndi mtendere, mukafundidwe ndipo mukakhute”, koma osaŵapatsa zimene akusoŵazo, pamenepo phindu lake nchiyani?
Choncho, chikhulupiriro pachokha, chopanda ntchito zake, nchakufa basi.
Koma kapena wina anganene kuti, “Inuyo muli ndi chikhulupiriro, ineyo ndili ndi ntchito zabwino.” Pamenepo ine nkumuyankha kuti, “Uyesetse kundiwonetsa chikhulupiriro chako chopanda ntchito zakecho, ine ndi ntchito zanga ndikuwonetsa chikhulupiriro changa.”
Inu mumakhulupirira kuti Mulungu ndi mmodzi yekha. Ai chabwino, mumakhoza, komatu ndi mizimu yoipa yomwe imakhulupirira zimenezi, imachitanso kunjenjemera.
Mwachitsanzo: munthu wina aloŵa mumsonkhano mwanu atavala mphete zagolide m'manja, alinso ndi zovala zokongola. Winanso nkuloŵa, koma ali mmphaŵi, nsanza zili wirawira.
Wopusawe, kodi ukufuna umboni wotsimikiza kuti chikhulupiriro chopanda ntchito zake nchachabe?
Nanga Abrahamu, kholo lathu, suja adakhala wolungama pamaso pa Mulungu chifukwa cha ntchito yomwe adachita, muja adaapereka mwana wake Isaki pa guwa lansembe?
Waona tsono kuti chikhulupiriro chake ndi zochita zake zidachitikira pamodzi. Zochita zake zidasandutsa chikhulupiriro chake kuti chifike pake penipeni.
Motero zidachitikadi zimene Malembo adaanena, kuti, “Abrahamu adakhulupirira Mulungu, nchifukwa chake Mulungu adamuwona kuti ngwolungama;” mwakuti ankatchedwa bwenzi la Mulungu.
Mukuwonatu kuti zochita zake za munthu ndizo zimamsandutsa wolungama pamaso pa Mulungu, osati chikhulupiriro chokha.
Kodi suja zidaateronso ndi Rahabu, mkazi wadama uja? Iye adaalandira azondi aja, nkuŵabweza kwao poŵadzeretsa njira ina, ndipo adapezeka kuti ngwolungama pamaso pa Mulungu chifukwa cha zimene adaachitazo.
Paja monga momwe thupi lopanda mzimu limakhala lakufa, moteronso chikhulupiriro chopanda ntchito zake nchakufa.
Tsono inu pofuna kusamala kwambiri wovala zokongolayo, mumuuza kuti, “Khalani apa pabwinopa”, mmphaŵi uja nkumuuza kuti, “Iwe, kaimirire apo, kapena dzakhale pansi kumapazi kwangaku.”
Limenelotu ndi tsankho pakati pa inu nokhanokha, ndipo inuyo mwasanduka oweruza a maganizo oipa.
Chauta adati, “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri: amayenda makosi ali wee, amayang'ana ndi maso ophika. Amayenda nyang'anyang'a ndi kuliza zigwinjiri zam'miyendo.
Nchifukwa chake Ambuye adzatulutsa zipere kumutu kwa akazi a ku Ziyoniwo, tsitsi lao lonse lidzatha phu!”
Tsiku limenelo Ambuye adzaŵachotsera zokongoletsera m'miyendo, kumutu ndi m'khosi,
maukufu, makoza, ndi nsalu zakumaso,
anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo, aweruzi ndi aneneri, olosa ndi akuluakulu,
maduku, zigwinjiri, malamba, mabotolo a zonunkhira, zithumwa,
mphete, zipini,
madelesi apaphwando, makepi, miinjiro, zikwama,
akalilole, zovala zabafuta, nduŵira, ndiponso nsalu zam'mapewa.
M'malo mwa kununkhira padzakhala kununkha, m'malo mwa lamba adzavala chingwe, m'malo mwa tsitsi lopesa bwino adzakhala ndi mipala, m'malo mwa delesi la mtengo wapatali adzavala chiguduli, m'malo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
Inunso anyamata, muzimvera akulu. Ndipo nonsenu, khalani okonzeka kutumikirana modzichepetsa. Paja mau a Mulungu akuti. “Mulungu amatsutsa odzikuza, koma amaŵakomera mtima anthu odzichepetsa.”
“Upangenso duŵa la golide wabwino kwambiri, ulembepo mozokota mau akuti, ‘Choperekedwa kwa Chauta.’
Musadzinyenge, nkosatheka kupusitsa Mulungu. Zimene munthu amabzala, adzakolola zomwezo.
Musamatsanzira makhalidwe a anthu odalira zapansipano, koma Mulungu asinthe moyo wanu wonse pakukupatsani mitima yatsopano. Pamenepo mudzatha kudziŵa zimene Mulungu afuna, ndipo mudzazindikira zimene zili zabwino, zangwiro ndi zomkondwetsa.
Mkazi ameneyu amasoka zovala za nsalu yabafuta, nazigulitsa, amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
Sindikunena zimenezi modandaula kuti ndikusoŵa kanthu, pakuti ine ndaphunzira kukhutira ndi zimene ndili nazo.
Kukhala wosauka ndimakudziŵa, kukhala wolemera ndimakudziŵanso. Pa zonse ndidaphunzira chinsinsi chake cha kukhala wokhutitsidwa, pamene ndapeza chakudya kapena ndili ndi njala, pamene ndili ndi zambiri kapena ndili wosoŵeratu.
“Nchifukwa chake musamada nkhaŵa nkumanena kuti, ‘Tidzadyanji? Tidzamwanji? Tidzavalanji?’
Paja zimenezi amazifunafuna ndi anthu akunja. Atate anu akumwamba amadziŵa kuti mukuzisoŵa zonsezi.
Mkango umene uli ndi mphamvu kupambana nyama zonse, ndipo suthaŵa kanthu kalikonse.
Tambala woyenda chinyachinya, ndi tonde, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
Pansi pano chinthu chilichonse chili ndi nyengo yake ndi nthaŵi yake yomwe adaika Mulungu:
Komabe chenjerani kuti ufulu wanuwu pochita zinthu, ungaphunthwitse ena amene chikhulupiriro chao nchosalimba kwenikweni.
Israele ankakonda Yosefe kupambana ana ake ena onse, popeza kuti anali mwana wake wapaukalamba. Adamsokera mkanjo wautali wamanja.
Usavutike munthu wina akamalemera, pamene chuma cha m'nyumba mwake chikukulirakulira.
Chifukwa pamene munthuyu amwalira, sadzatengapo kanthu. Chuma chake sichidzapita naye limodzi.
Uyang'ane pozungulira, uwone zimene zikuchitika. Anthu ako onse akusonkhana, akubwera kwa iwe. Pali Ine ndemwe, Mulungu wamoyo, anthu ako adzakhala chinthu chokukongoletsa. Udzaŵaonetsera monga amachitira mkwati wamkazi.
Umu ndi m'mene kale lija azimai oyera mtima okhulupirira Mulungu ankadzikongoletsera, ndipo ankamvera amuna ao.
Mudaliphimba ndi nyanja yozama ngati ndi chovala, ndipo madzi adakwera mpaka pamwamba pa mapiri.
Mutaŵadzudzula, madziwo adathaŵa, atamva mkokomo wa bingu lanu, adamwazika.
Mapiri adatumphuka, zigwa zidatsika, mpaka kumene Inu mudaakonzeratu.
Mu ufumu wa Mulungu chachikulu si chakudya kapena zakumwa ai, koma chilungamo, mtendere ndi chimwemwe, zimene Mzimu Woyera amapereka.
ndipo mwavala moyo watsopano. Moyo umenewu, Mlengi wanu akuukonzabe kosalekeza, kuti mudzamdziŵe kwenikweni ndi kufanafana naye.
Koma zipatso zimene Mzimu Woyera amabweretsa m'moyo wa munthu ndi izi: Chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, kukhulupirika,
kufatsa ndiponso kudziletsa. Zimenezi palibe lamulo loziletsa.
Kuli bwino kudyera masamba pali chikondi, kupambana kudyera nyama ya ng'ombe yonenepa pali chidani.
Anthu anjala muziŵagaŵirako chakudya chanu, osoŵa pokhala muziŵapatsako malo. Mukaona wausiŵa, mpatseni chovala, musalephere kuthandiza amene ali abale anu.
Amapereka chithandizo mwaufulu, amaoloŵa manja kwa anthu osauka. Chilungamo chake chidzakhala chamuyaya, adzakhala wamphamvu ndipo anthu adzampatsa ulemu.
“Umsokerenso Aroni mwinjiro wa bafuta wokoma, ndipo umpangire nduŵira ya bafuta wokoma, ndiponso lamba wopetedwa mokongola.
Ndikufuna kuti paliponse amuna popemphera azikweza manja ao kwa Mulungu momchitira ulemu, mopanda mkwiyo kapena kukangana.
Kukongola kwa achinyamata kwagona pa nyonga zao, koma ulemerero wa nkhalamba wagona pa imvi zao.
Momwe chimaonekera chipini chagolide chikakhala pa mpuno wa nkhumba, ndi momwenso kumakhalira kukongola kwa mkazi wam'kamwa.
“Nchifukwa chake ndikukuuzani kuti musamadera nkhaŵa moyo wanu, kuti mudzadyanji, kapena mudzamwanji, kapena thupi lanu, kuti mudzavalanji. Kodi suja moyo umaposa chakudya? Kodi suja thupi limaposa zovala?
Kwinaku mauwo amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamula anthu zambiri pa za kupembedza, za kudzichepetsa ndi za kuzunza thupi lao. Komabe malamulowo alibe phindu, ndipo sathandiza konse kugonjetsa khalidwe longosangalatsa thupi.
Kutemberera anzake kunali ngati chovala chake, motero matemberero amgwere ngati mvula. Akhale ngati mafuta oloŵa m'mafupa mwake.
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, kukongola nkosakhalitsa, koma mkazi woopa Chauta ndiye woyenera kumtamanda.
Motero palibe kusiyana pakati pa Ayuda ndi anthu a mitundu ina, pakati pa akapolo ndi mfulu, kapenanso pakati pa amuna ndi akazi, pakuti nonsenu ndinu amodzi mwa Khristu Yesu.
Musamalikonde dziko lapansi kapena zinthu zapansipano. Munthu akamakonda dziko lapansi, chikondi chokonda Atate sichikhalamo mwa iye.
Paja zonse zapansipano, zilakolako zathupi, zinthu zimene maso amakhumbira, ndiponso kunyadira za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku mkhalidwe woipa wa dziko lapansi.
“Pamene mfumu ija idaloŵa m'nyumbamo kukaona anthu odzadya phwando aja, idapezamo wina amene sadavale chovala chaukwati.
Tsono idamufunsa kuti ‘Kodi iwe, waloŵa bwanji muno opanda chovala chaukwati?’ Iye uja adangoti chete.
M'mapiri aatali ndimo m'mene mumakhala mbalale, m'matanthwe ndimo m'mene mumathaŵira mbira.
Ndinkayenda m'mbali mwa munda wa munthu waulesi, m'mbali mwa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
M'minda monsemo munali mutamera minga yokhayokha, m'nthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utagwa.
Wandituma kuti ndiŵakonzere zofunika olira a ku Ziyoni, ndiye kuti ndiŵapatse maluŵa achisangalalo m'malo mwa phulusa lachisoni, ndiŵapatse mafuta osonyeza kukondwa m'malo mwa kulira, ndiŵapatse chovala cha chikondwerero m'malo mwa kutaya mtima. Tsono adzatchedwa mitengo yamphamvu yachilungamo, yoibzala Chauta, kuti Iye mwini apezepo ulemu.
Ndithu ndikudziŵa mosakayika konse kuti palibe kanthu kangatilekanitse ndi chikondi chake. Ngakhale imfa kapena moyo, ngakhale angelo kapena olamulira, ngakhale zinthu zimene zilipo tsopano, kapena zimene zidzaoneke m'tsogolomo, kapena zamphamvu zina zilizonse,
ngakhale zakumwamba kapena zapansi, kapenanso kanthu kena kalikonse kolengedwa, sikangadzatilekanitse ndi chikondi cha Mulungu, chimene tili nacho mwa Khristu Yesu Ambuye athu.
Kodi simudziŵa kuti thupi lanu ndi nyumba ya Mzimu Woyera? Mulungu adakupatsani Mzimuyo kuti akhale mwa inu. Nchifukwa chake moyo umene muli nawo si wanunso.
Kodi simukudziŵa kuti akhristu ndiwo adzaweruza anthu onse? Tsono ngati inu mudzaweruza anthu onse, kodi simungathe kuweruza ngakhale ndi timilandu tating'ono tomwe?
Mulungu adakugulani ndi mtengo wapatali, tsono muzimlemekeza ndi matupi anu.
Aroni ndi ana ake azivala zimenezi nthaŵi zonse akamapita ku chihema chamsonkhano kapena ku guwa, kukanditumikira ku malo opatulika aja, kuwopa kuti angachimwe ndipo angafe. Lamulo limeneli, lonena za Aroni ndi zidzukulu zake, ndi lokhazikika mpaka muyaya.
Adzakuphimba ndi nthenga za mapiko ake, udzapeza malo othaŵirako m'mapikomo. Kukhulupirika kwake kumateteza monga chishango ndi lihawo.
Munthu satenga chigamba cha nsalu yatsopano, nkuchisokerera pa chovala chakale. Chigamba chotere chimakoka nkunyotsolako chovalacho, ndiye kung'ambika kwake kumakhala kwakukulu koposa kale.
Adapatsanso aliyense zovala zachikondwerero, koma Benjamini adampatsa mashikeli asiliva okwana 300, ndi zovala zisanu zachikondwerero.
Usakhale mmodzi mwa anthu opereka zikole, amene amasanduka chigwiriro cha ngongole.
Ngati ulephera kulipira, adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
Ndi ngati mafuta amtengowapatali oŵathira pa mutu, otsikira ku ndevu, ku ndevu za Aroni, oyenderera mpaka ku khosi la mkanjo wake.
Mwina Mulungu amamlemeretsa munthu pakumpatsa chuma ndi zabwino zina, namlola kuti akondwerere zonsezo. Munthuyo azilandire zimenezo ndi kumakondwerera ntchito zake zonse zolemetsa. Imeneyi ndi mphatso yochokeradi kwa Mulungu.
Mtendere wa Khristu uzikutsogolerani m'mitima mwanu. Mulungu adakuitanani kuti mukhale nawo mtendere umenewu, popeza kuti ndinu ziwalo za thupi limodzi. Muzikhala oyamika.
Mau a Khristu akhazikike kwathunthu m'mitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana ndi nzeru zonse. Muziimbira Mulungu ndi chiyamiko m'mitima mwanu, pamene mukuimba masalimo, nyimbo zotamanda Mulungu ndi nyimbo zina zauzimu.
Chauta, mtima wanga ndi wosadzikuza, maso anga ndi osanyada. Sinditengeka mtima ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.
Koma ndautonthoza ndi kuukhalitsa chete mtima wanga, monga mwana amene mai wake amamtonthoza ndi bere. Momwemo mtima wanga uli phe m'kati mwanga.
Munthu akakuzenga mlandu nafuna kukulanda mkanjo wako, umlole atengenso ndi mwinjiro wako womwe.
Nchifukwa chake tsono, nthaŵi zonse tikapeza mpata, tizichitira anthu onse zabwino, makamaka abale athu achikhristu.
M'malo mwa kununkhira padzakhala kununkha, m'malo mwa lamba adzavala chingwe, m'malo mwa tsitsi lopesa bwino adzakhala ndi mipala, m'malo mwa delesi la mtengo wapatali adzavala chiguduli, m'malo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
Iwe Yerusalemu, anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga, ndipo anthu ako amphamvu adzafera ku nkhondo.
Ife amene tili ndi chikhulupiriro champhamvu, tiziŵalezera mtima anthu ofooka, osamangodzikondweretsa tokha.
“Musadziwunjikire chuma pansi pano, pamene njenjete ndi dzimbiri zimaononga, ndiponso mbala zimathyola ndi kuba.
“Nchifukwa chake pamene mukupereka zachifundo, musachite modziwonetsera, monga amachitira anthu achiphamaso aja m'nyumba zamapemphero ndiponso m'miseu yam'mizinda. Iwoŵa amachita zimenezi kuti anthu aŵatame. Ndithu ndikunenetsa kuti amenewo alandiriratu mphotho yao.
Koma mudziwunjikire chuma Kumwamba, kumene njenjete kapena dzimbiri siziwononga, ndiponso mbala sizithyola ndi kuba.
Kuli bwino kudya mkute wouma pali bata, kuposa kuchita madyerero m'nyumba m'mene muli mikangano.
Musamachita kanthu ndi mtima wodzikonda, kapena wodzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa, ndipo aliyense aziwona anzake kuti ngomuposa iyeyo.
Chifukwa cha kugwira ntchito ya Khristu, iyeyu adaali pafupifupi kufa. Adaadzipereka osaopa ngakhale kutaya moyo wake kuti azindithandiza pa zimene inu simudathe kukwaniritsa pondithandiza.
Musamangofuna zokomera inu nokha, koma zokomeranso anzanu.
Koma mai wamasiye amene amangodzisangalatsa ndi zapansipano, ameneyo wafa kale ngakhale akali moyo.
Mmphaŵi ngakhale anzake omwe samukonda, koma wolemera amakhala ndi abwenzi ambiri.
Amene amanyoza mnzake ngwochimwa, koma ngwodala amene amachitira chifundo amphaŵi.
Mumameretsa udzu kuti ng'ombe zidye, ndi zomera kuti munthu azilima ndi kupeza chakudya m'nthaka.
Ngati uvomereza ndi pakamwa pako kuti Yesu ndi Ambuye, ndipo ukhulupirira mumtima mwako kuti Mulungu adamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka.
Motero Yakobe adauza banja lake ndi onse amene anali naye kuti, “Tayani milungu yachilendo imene muli nayo pakati panu. Mudziyeretse, ndipo muvale zovala zaudongo.
Koma tsopano Chauta amene adakulenga iwe Yakobe, amene adakuumba iwe Israele, akunena kuti, “Usaope, chifukwa ndidakuwombola, ndidachita kukutchula dzina lako, ndiwe wanga.
Ndapempha chinthu chimodzi chokha kwa Chauta, chinthu chofunika kwambiri, chakuti ndizikhala m'Nyumba ya Chauta masiku onse a moyo wanga, kuti ndizikondwera ndi kukoma kwake kwa Chauta ndi kuti ndizipembedza Iye m'Nyumba mwakemo.
Wokomera mtima anthu osauka amachita ngati wokongoza Chauta, ndipo ndi Chautayo amene adzambwezera chifukwa cha ntchito zake.
Ndidaali wamaliseche, inu nkundiveka. Ndinkadwala, inu nkumadzandizonda. Ndidaali m'ndende, inu nkumadzandichezetsa.’
Pajatu nonsenu amene mudasanduka amodzi ndi Khristu pakubatizidwa, mudachita ngati kuvala moyo wa Khristu.
Motero palibe kusiyana pakati pa Ayuda ndi anthu a mitundu ina, pakati pa akapolo ndi mfulu, kapenanso pakati pa amuna ndi akazi, pakuti nonsenu ndinu amodzi mwa Khristu Yesu.
Amagwetsa chisanu chambee ngati ubweya. Amamwaza chipale ngati phulusa.
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
Akalamula kuti zichoke, pomwepo zimasungunuka, akaombetsa mphepo, madzi amayenda.