Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

110 Mau a Mulungu Okhudza Kuyeretsedwa

Ndikufuna ndikuuzani nkhani ya chiyeretso. Cholinga chachikulu cha chiyeretso ndicho kuchotsa chilichonse chimene chimatiletsa kwa Mulungu ndikubwezeretsa ubwenzi wathu ndi Iye. Ndi njira yofunika kuti tiyandikire ku chiyeretso ndikukhala motsatira malamulo ndi mawu ake.

Tikudziwa kuti Mulungu ndi woyera komanso wolungama, ndipo amatiitana kuti tikhale oyera monga momwe Iye alili woyera. Choncho, ndikofunikira tsiku lililonse kuti tiyandikire kwa Yesu kuti atiyeretse ndi mwazi wake woyera, chifukwa chiyeretso chenicheni chimachokera mkati, mumtima.

Ndicho chifukwa chake Yesu amatiitana kuti tiyang'ane zolinga zathu ndi zokhumba zathu zamkati, ndikulola Mzimu Woyera kuti uyeretse maganizo ndi malingaliro athu. Chiyeretso chimadalira kusintha kosalekeza m'moyo wa wokhulupirira aliyense.

M'mawa uliwonse timakumana ndi mavuto ndi mayesero omwe angasokoneze ubwenzi wathu ndi Mulungu. Ndikofunikira kukhala ndi mtima wofuna chiyeretso nthawi zonse ndikulapa, kukhulupirira chisomo ndi chikhululukiro chomwe Mulungu amatipatsa kudzera mwa Yesu.

Mu chiyeretso timapeza ufulu, poti timadzimasula ku uchimo ndi zisankho zolakwika. Timakhala oyandikira kwambiri ndi Mulungu ndikusangalala ndi ubwenzi wozama ndi Mlengi wathu.


Masalimo 51:7

Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzakhala woyera. Mundisambitse, ndipo ndidzayera kupambana chisanu chambee.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 51:10

Mundilengere mtima woyera, Inu Mulungu, muike mwa ine mtima watsopano ndi wokhazikika.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 9:14

Nanji tsono magazi a Khristu, angathe kuchita zoposa. Mwa Mzimu wamuyaya Iye adadzipereka ngati nsembe yopanda chilema kwa Mulungu. Ndiye kuti magazi ake adzayeretsa mitima yathu pakuichotsera ntchito zosapindulitsa moyo, kuti tizitumikira Mulungu wamoyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:8

Yandikirani kwa Mulungu, ndipo Iye adzayandikira kwa inu. Muzisamba m'manja, inu anthu ochimwa. Chotsani maganizo onyenga m'mitima mwanu, inu anthu okayikakayika.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 7:1

Tsono, inu okondedwa, popeza kuti tili ndi malonjezo ameneŵa, tiyeni tidzichotsere zinthu zonse zodetsa thupi lathu kapena mtima wathu. Ndipo pakuwopa Mulungu tiziyesetsa ndithu kukhala oyera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 51:1-2

Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, malinga ndi chikondi chanu chosasinthika. Mufafanize machimo anga, malinga ndi chifundo chanu chachikulu.

Mundilengere mtima woyera, Inu Mulungu, muike mwa ine mtima watsopano ndi wokhazikika.

Musandipirikitse pamaso panu, musachotse Mzimu wanu woyera mwa ine.

Mundibwezere chimwemwe cha chipulumutso chanu, mulimbitse mwa ine mtima womvera.

Pamenepo ochimwa ndidzaŵaphunzitsa njira zanu, ndipo iwo adzabwerera kwa Inu.

Mundikhululukire mlandu wanga wokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu Mpulumutsi wanga, ndipo ndidzakweza mau poimba za chipulumutso chanu.

Ambuye, tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalankhula zotamanda Inu.

Si nsembe wamba imene Inu imakusangalatsani. Ndikadapereka nsembe yopsereza, sibwenzi Inu mutakondwera nayo.

Nsembe imene Inu Mulungu mumailandira, ndi mtima wotswanyika. Mtima wachisoni ndi wolapa, Inu Mulungu simudzaunyoza.

Muŵachitire zabwino anthu a ku Ziyoni, chifukwa cha kukoma mtima kwanu. Mumangenso kachiŵiri makoma a Yerusalemu.

Pamenepo mudzakondwera ndi nsembe zoyenera, nsembe zootcha ndi zopsereza kwathunthu. Choncho adzapereka ng'ombe zamphongo pa guwa lanu lansembe.

Mundisambitse kwathunthu pochotsa kulakwa kwanga, mundiyeretse mtima pochotsa machimo anga.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 1:9

Koma tikamavomera kuti ndife ochimwa, Mulungu amene ali wokhulupirika ndi wolungama, adzatikhululukira machimo athuwo. Adzatiyeretsa ndi kutichotsera kusalungama kwathu konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 1:18

Chauta akunena kuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu: chifukwa cha machimo anu mwafiira kwambiri, koma Ine ndidzakutsukani, inu nkukhala oyera kuti mbee. Mwachita kuti psuu ngati magazi, koma mudzakhala oyera ngati thonje.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 1:16

Sambani, dziyeretseni, chotsani pamaso panga ntchito zanu zoipa. Inde, lekani kuchita zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 36:25-26

Ndidzakuwazani madzi angwiro, ndipo mudzayera, zonse zokuipitsani zidzachoka. Ndiponso ndidzakuyeretsani pochotsa mafano anu onse.

Ndidzakupatsani mtima watsopano ndi kuloŵetsa mzimu watsopano mwa inu. Ndidzakuchotserani mtima wanu wouma ngati mwalawo ndi kukupatsani mtima wofeŵa ngati mnofu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:2-3

Inu okondedwa, ndife ana a Mulungu tsopano. Mulungu sadatiwonetsebe chimene tidzakhale. Koma tikudziŵa kuti Iye akadzaoneka, tidzakhala ofanafana naye, pakuti tidzamuwona monga momwe aliri.

nthaŵi zonse pamene mtima wathu ukutitsutsa kuti ndife olakwa. Paja Mulungu ndi wamkulu kopambana mtima wathu, ndipo amadziŵa zonse.

Inu okondedwa, ngati mtima wathu sutitsutsa, titha kuima mopanda mantha pamaso pa Mulungu.

Ndipo chilichonse chimene timpempha, amatipatsa, chifukwa timatsata malamulo ake, ndipo timachita zomkondweretsa.

Chimene Mulungu amalamula nchakuti tizikhulupirira Mwana wake Yesu Khristu, ndipo kuti tizikondana monga Iye adatilamulira.

Munthu wotsata malamulo a Mulungu, amakhala mwa Mulungu, ndipo Mulungu amakhala mwa iye. Chifukwa cha Mzimu Woyera amene adatipatsa, timadziŵa kuti Mulungu amakhaladi mwa ife.

Munthu aliyense amene ali ndi chiyembekezo chimenechi pa Khristu, amadzisandutsa woyera monga momwe Khristuyo ali woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Tito 2:14

Paja Iye adadzipereka chifukwa cha ife, kuti atipulumutse ku zoipa zathu zonse, ndi kutiyeretsa kuti tikhale anthu ake achangu pa ntchito zonse zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:25-26

Inu amuna, muzikonda akazi anu, monga momwe Khristu adakondera Mpingo, nadzipereka chifukwa cha Mpingowo.

Adachita zimenezi kuti aupatule ukhale wakewake, atauyeretsa pakuutsuka ndi madzi ndiponso ndi mau ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 22:16

Nanga tsono ukuchedweranji? Dzuka ndi kutama dzina lake mopemba, ubatizidwe ndi kusambitsidwa kuti machimo ako achoke.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 1:22

Mwayeretsa mitima yanu pakumvera choona, kotero kuti muzikondana ndi akhristu anzanu mosanyenga. Nchifukwa chake muzikondana ndi mtima wonse, mosafookera.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:3

Munthu aliyense amene ali ndi chiyembekezo chimenechi pa Khristu, amadzisandutsa woyera monga momwe Khristuyo ali woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:9

Kodi mnyamata angathe bwanji kusunga makhalidwe ake kuti akhale angwiro? Akaŵasamala potsata mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 30:12

Pali ena amene amadziyesa oyera mtima, koma sadachotse zoipa zao.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:8

Ngodala anthu oyera mtima, pakuti adzaona Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 1:3

Iye ndiye kuŵala koonetsa ulemerero wa Mulungu, ndipo ndiye chithunzi chenicheni chosonyeza khalidwe la Mulungu. Iyeyu amachirikiza zonse ndi mau ake amphamvu. Atayeretsa mtundu wa anthu pakuŵachotsa machimo, adakakhala Kumwamba, ku dzanja lamanja la Mulungu waulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:21

Madziwo akufanizira ubatizo umene masiku ano umakupulumutsani chifukwa cha kuuka kwa Yesu Khristu. Kubatizidwa kumeneku si kuchotsedwa litsiro la m'thupi, koma kudzipereka kwa Mulungu ndi mtima woona, kudzera mwa Yesu Khristu

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 66:10

Inu Mulungu, mwatiyesa, mwatiyeretsa monga m'mene amayeretsera siliva.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 6:11

Enanu munali otere kale, koma mudayeretsedwa, mudasanduka anthu a Mulungu, ndipo mudapezeka olungama pamaso pake. Zimenezi zidachitika m'dzina la Ambuye Yesu Khristu, ndiponso mwa Mzimu wa Mulungu wathu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yoswa 24:23

Yoswa adatinso, “Chotsani milungu yachilendo imene ili pakati panu, ndipo muzipembedza Chauta, Mulungu wa Israele, mokhulupirika.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 24:3-4

Ndani angayenere kukwera phiri la Chauta? Ndani angaime m'malo ake oyera?

Ndi amene amachita zabwino ndi manja ake, ndipo amaganiza zabwino mumtima mwake. Ndi amene salingalira zonama, ndipo salumbira monyenga.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 1:9

Paja munthu wopanda zimenezi ndiye kuti ngwakhungu, sangathe kuwona patali, ndipo waiŵala kuti adamtsuka machimo ake akale.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 6:6-7

Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja adaulukira kwa ine, ali ndi khala lamoto m'manja mwake. Khalalo adaalichotsa pa guwa la nsembe ndi mbaniro.

Ndipo adandikhudza pakamwa ndi khala lamotolo nati, “Taona, ndakukhudza milomo ndi khalali. Kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:3

Inu mwayera kale chifukwa cha mau amene ndakuuzani.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:26

Adachita zimenezi kuti aupatule ukhale wakewake, atauyeretsa pakuutsuka ndi madzi ndiponso ndi mau ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:1-2

Tsono abale, popeza kuti Mulungu watichitira chifundo chachikulu chotere, ndikukupemphani kuti mupereke matupi anu omwe kuti akhale nsembe yamoyo, yopatulika, ndi yokondwetsa Mulungu. Imeneyi ikhale njira yanu yopembedzera Mulungu mwauzimu.

Muzikondana kwenikweni monga abale, ndipo muzichita ngati kupikisana poonetsana ulemu.

Potumikira Ambuye, changu chanu chisazilale, koma chikhalebe choyaka.

Muzikhala okondwa chifukwa cha chiyembekezo chanu. Muzipirira pakati pa masautso, ndipo muzipemphera nthaŵi zonse.

Muzipereka zothandiza akhristu anzanu osoŵa, ndipo muziyesetsa kulandira alendo mokondwa.

Pemphani Mulungu kuti aŵadalitse amene amakuzunzani. Ndithu, pemphani kuti aŵadalitse, osaŵatemberera ai.

Muzikondwa nawo amene akukondwa, muzilira nawo amene akulira.

Muzimvana bwino, ndipo musamadzikweze, koma muziyanjana nawo anthu wamba. Musamadziyese anzeru.

Munthu akakuchitani choipa, musamubwezere choipa. Yesani kuchita zimene anthu onse amaziwona kuti nzabwino.

Ngati nkotheka, khalani ndi mtendere ndi anthu onse, monga momwe mungathere.

Okondedwa anga, musabwezere choipa, koma alekeni, mkwiyo wa Mulungu ndiwo uŵalange. Paja Malembo akuti, “Kulipsira nkwanga. Ndidzaŵalanga ndine, akutero Chauta.”

Musamatsanzira makhalidwe a anthu odalira zapansipano, koma Mulungu asinthe moyo wanu wonse pakukupatsani mitima yatsopano. Pamenepo mudzatha kudziŵa zimene Mulungu afuna, ndipo mudzazindikira zimene zili zabwino, zangwiro ndi zomkondwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 9:23

Tsono padaafunika kuti zinthu zongofanizira zenizeni za Kumwamba, ziyeretsedwe ndi miyambo imeneyi. Koma kuti za Kumwamba zenizenizo ziyeretsedwe, padaafunika nsembe zina zoposa zimenezo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:23-24

Fufuzeni, Inu Mulungu, kuti mudziŵe mtima wanga. Yeseni kuti mudziŵe maganizo anga.

Muwone ngati ndimatsata njira yoipa iliyonse, ndipo munditsogolere m'njira yanu yamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 15:9

Mulungu sadasiyanitse konse pakati pa ife ndi iwo, koma adayetsera mitima yao ndi chikhulupiriro chao.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 36:25

Ndidzakuwazani madzi angwiro, ndipo mudzayera, zonse zokuipitsani zidzachoka. Ndiponso ndidzakuyeretsani pochotsa mafano anu onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:22

Nchifukwa chake tsono, tiyeni tiyandikire kwa Mulungu ndi mtima woona, tili ndi chitsimikizo cha chikhulupiriro. Timuyandikire ndi mitima yoyeretsedwa, yopanda kalikonse koitsutsa, ndiponso ndi matupi osambitsidwa ndi madzi oyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 33:8

Ndidzaŵayeretsa pochotsa machimo ao onse ondichimwira. Ndidzaŵakhululukira zoipa zonse zimene adachita pondipandukira.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 36:29

Ndidzakupulumutsani ku zonse zokuipitsani. Ndidzakuchulukitsirani tirigu, ndipo sindidzakugwetseraninso njala.

Mutu    |  Mabaibulo
Malaki 3:3

Adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri wapang'anjo woyeretsa siliva, ndipo adzayeretsa Alevi monga amayeretsera golide ndi siliva, mpaka kuti azidzapereka nsembe zoyenera kwa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 16:30

Pajatu pa tsiku limenelo padzakhala mwambo wopepesera machimo anu, kuti machimo anu achotsedwe. Choncho mudzakhala oyera pamaso pa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 13:1

Chauta Wamphamvuzonse akunena kuti, “Tsiku limenelo banja la Davide adzalikonzera kasupe wa madzi, kuti iwo pamodzi ndi anthu a ku Yerusalemu aŵachotsere machimo ao ndi zoipa zao.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:9

Koma inu ndinu fuko losankhidwa, ansembe achifumu, mtundu wopatulika, anthu akeake a Mulungu. Adakusankhani kuti mukalalike ntchito zamphamvu za Iye amene adakuitanani kuti mutuluke mu mdima, mukaloŵe m'kuŵala kwake kodabwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:9

Ndani angathe kunena kuti, “Ine ndauyeretsa mtima wanga, ndilibenso tchimo lililonse.”

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 3:11

“Ine ndimakubatizani ndi madzi, kusonyeza kuti mwatembenuka mtima. Koma amene akubwera pambuyo panga ndi wamphamvu kuposa ine. Ameneyo ine ndine wosayenera ngakhale kunyamula nsapato zake. Iyeyo adzakubatizani mwa Mzimu Woyera ndiponso m'moto.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 2:21

Tsono munthu akadziyeretsa nkusiya zotsikazi, adzakhala ngati chiŵiya cha ntchito zolemerera. Adzakhala wopatulika ndi wofunika zedi kwa Ambuye ake, wokonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:18

Munthu amene ali ndi chikondi, alibe mantha, pakuti chikondi changwiro chimatulutsira mantha kunja. Munthu akamachita mantha, ndiye kuti akuwopa chilango, ndipo chikondi sichidafike pake penipeni mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:8

Chachikulu nchakuti muzikondana mosafookera, popeza kuti chikondi chimaphimba machimo ochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 30:18-21

“Upange beseni lamkuŵa losambira, ndipo phaka lake likhale lamkuŵa. Ulikhazike pakati pa chihema chamsonkhano ndi guwa, ndipo uthiremo madzi.

Aroni ndi ana ake azisamba m'manja ndi kutsuka mapazi ao ndi madzi amenewo.

Likhale lalibanda, kutalika kwake masentimita 46, muufupi mwake likhalenso masentimita 46, ndipo msinkhu wake ukhale wa masentimita 91. Nyanga zake zipangidwire kumodzi ndi guwalo.

Akamaloŵa m'chihema chamsonkhano, kapena kuyandikira guwalo pa ntchito yao yautumiki, ndi kumapereka kwa Chauta chopereka chopsereza, sadzafa malinga akasamba ndi madzi amenewo.

Azisamba m'manja ndi kutsuka mapazi, kuti angafe. Limeneli ndi lamulo ndithu limene iwowo ndi adzukulu ao akutsogolo ayenera kumadzalitsata mpaka muyaya.”

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 14:9

Pa tsiku lotsiriza amete tsitsi lake lonse kumutu. Ametenso ndevu zake pamodzi ndi nsidze zomwe, tsitsi lake lonse ndithu. Kenaka achape zovala zake ndi kusamba, ndipo atatero, adzakhala woyeretsedwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 51:2

Mundisambitse kwathunthu pochotsa kulakwa kwanga, mundiyeretse mtima pochotsa machimo anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 36:33

“Zimene ndikunena Ine Ambuye Chauta ndi izi: Pamene ndidzachotsa machimo anu, ndidzaikamonso anthu m'mizindamo, ndipo ndidzamanganso nyumba pa mabwinja aja.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 4:4

Pamenepo Ambuye adzakhala atasambitsa akazi a ku Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zao, ndipo adzakhala atatsuka magazi amene adakhetsedwa mu Yerusalemu. Adzachita zimenezi ndi mpweya woweruza ndi woyeretsa ndi moto.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 1:5

Akukomereninso mtima ndi kukupatsani mtendere Yesu Khristu, mboni yokhulupirika, amene ali woyambirira kulandira moyo waulemerero, amenenso ali Mfumu yolamula mafumu onse a pa dziko lapansi. Iyeyo amatikonda, ndipo ndi magazi ake adatimasula ku machimo athu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 5:7

Muchotse chofufumitsira chakalechi cha uchimo, kuti mukhale oyera mtima ndithu, ngati buledi watsopano wosafufumitsa, monga momwe muliri ndithu, pakuti Khristu, Mwanawankhosa wathu wa Paska, adaphedwa kale ngati nsembe.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 11:44

Ine ndine Chauta, Mulungu wanu. Tsono mudziyeretse, ndipo mukhale oyera pakuti Ine ndine woyera. Musadziipitse ndi chinthu chokwaŵa pansi chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:14

Yesetsani kukhala ndi mtendere ndi anthu onse, ndi kukhala oyera mtima, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe amene adzaona Ambuye popanda kuyera mtimako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 66:18-19

Ndikadazindikira choipa chilichonse mumtima mwanga ndi kuchibisa, Ambuye sakadandimvera.

Koma zoonadi, Mulungu wandimvera, wasamala mau a pemphero langa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:23

Mtima wako uziwulonda bwino, pakuti m'menemo ndimo muli magwero a moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 4:7

Paja Mulungu sadatiitane kuti tizichita zonyansa, koma kuti tikhale oyera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 9:22

Malinga ndi Malamulo a Mosewo pafupifupi zonse zimayeretsedwa ndi magazi, ndipo machimo sakhululukidwa popanda kukhetsa magazi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 1:5

Cholinga changa pokupatsa malangizo ameneŵa, nchakuti pakhale chikondi chochokera mu mtima woyera, mu mtima wopanda kanthu koutsutsa, ndiponso m'chikhulupiriro chopanda chiphamaso.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 8:2-3

Tsono munthu wina wakhate adadzamugwadira nati, “Ambuye, mutafuna mungathe kundichiritsa.”

Yesu adamuyankha kuti, “Nkhandwe zili ndi michembo yake, mbalame zili ndi zisa zake, koma Mwana wa Munthu alibe mpogoneka mutu pomwe.”

Wophunzira wake wina adauza Yesu kuti, “Ambuye, mundilole ndiyambe ndakaika maliro a atate anga.”

Koma Yesu adamuuza kuti, “Iweyo unditsate, aleke akufa aziika akufa anzao.”

Yesu adaloŵa m'chombo, ndipo ophunzira ake adatsagana naye.

Tsono padauka namondwe woopsa panyanjapo, kotero kuti mafunde ankaloŵa m'chombomo. Koma Yesu anali m'tulo.

Pamenepo ophunzira ake aja adamudzutsa, adati, “Ambuye, tipulumutseni, tikumiratu!”

Apo Yesu adaŵafunsa kuti, “Bwanji mukuchita mantha, inu anthu a chikhulupiriro chochepa?” Atatero adaimirira nkudzudzula mphepoyo ndi nyanjayo, kenaka padagwa bata lalikulu ndithu.

Ophunzira aja adazizwa nati, “Kodi ameneyu ndi munthu wotani kuti ngakhale mphepo ndi nyanja yomwe zizimumvera?”

Yesu atafika ku tsidya la nyanja, ku dera la Agadara, anthu aŵiri ogwidwa ndi mizimu yoipa adadzakumana naye kuchokera ku manda. Anali aukali kwambiri, kotero kuti panalibe munthu ndi mmodzi yemwe wotha kudzera njira imeneyo.

Mwadzidzidzi anthuwo adayamba kufuula kuti, “Kodi takuputani chiyani, Inu Mwana wa Mulungu? Kodi mwabwera kuno kudzatizunza nthaŵi isanakwane?”

Yesu adatambalitsa dzanja nkumukhudza, nati, “Chabwino, ndikufuna, chira!” Pomwepo khate lake lija lidatha, ndipo adachiradi.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:10

Chifukwa chakuti Yesu Khristu adachita zimene Mulungu adaafuna kuti achite, ife tidayeretsedwa ndi nsembe ya thupi lake, limene Iye adapereka kamodzi kokhako.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 19:10

Chauta adauza Mose kuti, “Pita kwa anthuwo, ndipo uŵayeretse lero ndi maŵa. Achape zovala zao,

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 7:14

Ine ndidati, “Mbuyanga, mukudziŵa ndinu.” Ndipo iye adandiwuza kuti, “Ameneŵa ndi amene adapambana m'masautso aakulu aja. Adachapa mikanjo yao ndi kuiyeretsa m'magazi a Mwanawankhosa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:27

Chipembedzo choona ndi changwiro pamaso pa Mulungu amene ali Atate, ndi ichi: kusamalira ana amasiye ndi akazi amasiye pa mavuto ao, ndiponso kudzisunga bwino, kuwopa kudetsedwa ndi zoipa za m'dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 6:6-7

Tidziŵa kuti mkhalidwe wathu wakale udapachikidwa pa mtanda pamodzi ndi Khristu, kuti khumbo lathu lokonda machimo liwonongeke, ndipo tisakhalenso akapolo a uchimo.

Pakuti munthu akafa, ndiye kuti wamasuka ku mphamvu ya uchimo.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:22

Koma tsopano, kudzera mwa imfa ya Mwana wake m'thupi lake, Mulungu wakuyanjanitsaninso ndi Iye mwini. Adachita zimenezi kuti pamaso pake muthe kuwoneka muli oyera mtima, opanda banga kapena cholakwa chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:23

Mulungu mwini, amene amatipatsa mtendere, akusandutseni angwiro pa zonse. Akusungeni athunthu m'nzeru, mumtima ndi m'thupi, kuti mudzakhale opanda chilema pobwera Ambuye athu Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 3:5

Yesu adati, “Ndithu ndikunenetsa kuti ngati munthu sabadwa m'madzi ndi mwa Mzimu Woyera, sangathe kuloŵa mu Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:14

Mwa nsembe imodzi yomweyo wasandutsa angwiro kwamuyaya onse amene Iye akuŵayeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 73:1

Zoonadi, Mulungu ndi wabwino kwa olungama, kwa anthu oyera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 17:11

Pakuti moyo wake wa cholengedwa chilichonse uli m'magazi, ndipo ndaŵapereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amene amachotsa machimo, chifukwa cha moyo umene umakhala m'magazimo.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mafumu 5:10

Tsono Elisa adamtumira wamthenga kukamuuza kuti, “Pitani mukasambe mu mtsinje wa Yordani kasanunkaŵiri, ndipo muchira ndi kuyeretsedwa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 11:4

Iwe umati mau akowo ndi oona, ukuti ndiwe wangwiro pamaso pa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 3:4

Tsono mngeloyo adauza anzake omperekeza kuti, “Mvuleni zovala zake zalitsirozi.” Kenaka adauza Yoswa kuti, “Ona ndakuchotsera machimo ako, tsopano ndikuveka zovala zokongola.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:12-13

Nanga ndani angathe kudziŵa zolakwa zake? Inu Chauta, mundichotsere zolakwa zanga zobisika.

Musalole kuti ine mtumiki wanu ndizichimwa dala, kulakwa koteroku ndisakutsate. Tsono ndidzakhala wangwiro wopanda mlandu wa uchimo waukulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 40:30-32

Kenaka adaika beseni losambira lija pakati pa chihema chamsonkano ndi guwa, nathiramo madzi osamba.

Apo Mose, Aroni ndi ana ake adasamba m'manja natsuka mapazi ao.

Nthaŵi zonse akaloŵa m'chihema chamsonkhanomo, kapena kusendera ku guwalo, ankasamba, monga momwe Chauta adalamulira Mose.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 16:19

Awazeko magazi ena pamwamba pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kaŵiri, kuti alipatule ndi kuliyeretsa pochotsa machimo a Aisraele.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:1

Motero tsopano palibiretu mlandu wotsutsa anthu amene amakhala mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:11

Ndasunga mau anu mumtima mwanga, kuti ndisakuchimwireni.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:4

Khalani mwa Ine, ndipo Inenso ndidzakhala mwa inu. Nthambi siingathe kubala zipatso payokha ngati siikhala pa mtengo wake. Momwemonso inu ngati simukhala mwa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:6

Sindikayika konse kuti Mulungu, amene adayamba kuchita ntchito yabwinoyi mwa inu, adzaipitiriza mpaka itatsirizika pa Tsiku la Kubweranso kwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 9:13-14

Magazi a atonde ndi a ng'ombe zamphongo, ndiponso phulusa la mwanawang'ombe wamkazi zimawazidwa pa anthu amene ali odetsedwa chifukwa chosasamala mwambo wachiyuda. Zimenezi zimaŵayeretsa pakuŵachotsa litsiro lam'thupi.

Nanji tsono magazi a Khristu, angathe kuchita zoposa. Mwa Mzimu wamuyaya Iye adadzipereka ngati nsembe yopanda chilema kwa Mulungu. Ndiye kuti magazi ake adzayeretsa mitima yathu pakuichotsera ntchito zosapindulitsa moyo, kuti tizitumikira Mulungu wamoyo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 3:13

Motero Iye adzalimbitsa mitima yanu kuti idzakhale yangwiro ndi yoyera pamaso pa Mulungu Atate athu, pamene Ambuye Yesu adzabwerenso pamodzi ndi oyera ake onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:16

pakundipatula kuti ndikhale mtumiki wa Khristu Yesu kwa anthu a mitundu ina. Adandipatsa ntchito yolalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu ngati wansembe, kuti anthuwo akhale ngati nsembe yokomera Iye ndi yoperekedwa mwa Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 23:25-26

“Muli ndi tsoka, inu aphunzitsi a Malamulo ndi Afarisi, anthu achiphamaso! Mumatsuka kunja kwa chikho ndi kwa mbale koma m'kati mwake m'modzaza ndi nzeru zakuba, ndi zaumbombo.

Afarisi akhungu inu, yambani mwatsuka m'kati mwa chikho, ndipo kunja kwakenso kudzayera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 17:17

Muziŵapatula ndi mau anu kuti akhale anthu anu. Mau anuwo ngoona zedi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:24

Ndipo muvale moyo watsopano, umene Mulungu adaulenga, wofanafana naye. Apo mudzakhala olungama ndi oyera mtima kwenikweni.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 32:5

Koma ndidavomera tchimo langa kwa Inu, sindidabise kuipa kwanga. Ndidati, “Ndidzaulula machimo anga kwa Chauta,” pomwepo Inu mudakhululukiradi mlandu wa machimo anga.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:6

Yesu Khristu ndiye amene adabwera kudzera mwa madzi ndi mwa magazi. Sadabwere mwa madzi okha, koma mwa madzi ndi mwa magazi omwe. Ndipo Mzimu Woyera ndiye amene amachitirapo umboni, pakuti Mzimuyo ndiye choona.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 7:1

Tsopano ndiyankhe zimene mudandifunsa m'kalata yanu. Nkwabwino kuti munthu asakwatire,

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 1:4

Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo adatipatsa madalitso aakulu ndi amtengowapatali amene Iye adatilonjeza. Adatero kuti mulandireko moyo wake wa Mulungu, mutapulumuka ku chivunde chimene chili pa dziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 22:14

Ngodala amene amachapa mikanjo yao, kuti aloledwe kudya zipatso za mtengo wopatsa moyo, ndiponso kuloŵa mu mzinda kudzera pa zipata zija.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 6:22

Koma tsopano mwamasulidwa ku uchimo, ndipo ndinu otumikira Mulungu. Phindu lake ndi kuyera mtima, ndipo potsiriza pake kulandira moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 51:1

Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, malinga ndi chikondi chanu chosasinthika. Mufafanize machimo anga, malinga ndi chifundo chanu chachikulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:4

Mulungu asanalenge dziko lapansi, adatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi opanda cholakwa pamaso pake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 26:6

Ndimasamba m'manja kuwonetsa kuti sindidachimwe, ndimakupembedzani pa guwa lanu lansembe, Inu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 2:20

Ndidapachikidwa pa mtanda pamodzi ndi Khristu, kotero kuti sindinenso amene ndili ndi moyo, koma ndi Khristu amene ali ndi moyo mwa ine. Moyo umene ndili nawo tsopano m'thupi lino, ndi moyo wokhulupirira Mwana wa Mulungu, amene adandikonda napereka moyo wake chifukwa cha ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 20:26

Muzikhala oyera pamaso panga, pakuti Ine Chauta ndine woyera, ndipo ndakupatulani pakati pa anthu onse kuti mukhale anthu anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:2

Anthu opembedza Mulungu aja akadayeretsedwa kwathunthu, sibwenzi mtima wao ukuŵatsutsabe, ndipo akadaleka kumapereka nsembe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 52:11

Nyamukani, nyamukani, chokaniko msanga ku Babiloniko, musakhudze kanthu konyansa pa chipembedzo. Tulukanimo ndipo mudziyeretse, inu amene mukunyamula ziŵiya zopatulikira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:13-14

Adatilanditsa ku mphamvu za mdima wa zoipa, nkutiloŵetsa mu Ufumu wa Mwana wake wokondedwa.

Mwa Iyeyu Mulungu adatiwombola, ndiye kuti adatikhululukira machimo athu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:8

Inunso kale mudaali mu mdima, koma tsopano muli m'kuŵala, popeza kuti ndinu ao a Ambuye. Tsono muziyenda ngati anthu okhala m'kuŵala.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:15

kuti mukhale angwiro ndi osalakwa, ana a Mulungu opanda chilema chilichonse pakati pa anthu onyenga ndi osokeretsa anzao. Pakati pa anthu otere mumaŵala monga momwe zimaonekera nyenyezi pa dziko lapansi,

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 13:10

Yesu adamuuza kuti, “Munthu amene wasamba, wayera yense. Palibe chifukwa choti asambenso, koma kungosamba mapazi okha basi. Tsono inu mwayera, koma osati nonsenu ai.”

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 2:13

Pa mbali yathu, timathokoza Mulungu kosalekeza. Timatero chifukwa chakuti pamene mudamva mau a Mulungu amene tidakulalikirani, mudaŵalandira osati ngati mau a anthu chabe, koma monga momwe aliri ndithu, mau a Mulungu. Mauwo ndi omwe akugwira ntchito mwa inu okhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:7-8

Tsono muzigonjera Mulungu. Satana muzilimbana naye, ndipo adzakuthaŵani.

Yandikirani kwa Mulungu, ndipo Iye adzayandikira kwa inu. Muzisamba m'manja, inu anthu ochimwa. Chotsani maganizo onyenga m'mitima mwanu, inu anthu okayikakayika.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga, inu mumadziwa moyo wanga, ndikudziwa bwino kuti palibe chomwe ndingaise m'maso mwanu. Sindinanene mawu koma inu mumadziwa kale zonse zomwe ndikufuna kukuuzani. Lero ndikudzipereka pamaso panu, ndikuvomereza kuti ndinu mlengi wanga ndi mpulumutsi wanga. Zikomo chifukwa cha kukoma mtima kwanu pa ine ngakhale machimo anga ndi kuipa kwanga. Ndikubwera kwa inu Ambuye, ndikudziwa kuti ndikukusowani, kuti popanda inu sindingathe kukhala. Ndikukupemphani muchotse m'moyo wanga chilichonse chomwe chimandiletsa kukhala pafupi nanu. Munditsukitse ndi magazi anu, mundiyere ndi hisopo, ndipo ngakhale machimo anga ali ofiira ngati nsalu yofiira, muwachititse oyera ngati ubweya. Inu muli ndi mphamvu zosintha moyo wanga ndi kundipanga kukhala munthu watsopano. Atate, ndili m'manja mwanu achikondi, ndikungofuna kukukhutiritsani ndi kuchita chifuniro chanu. Mundipatule ndi magazi anu Yesu, ndipo mundithandize kukhala m'chiyero. Mundipatse mphamvu zanu kuti ndisagonje, munditeteze kuti ndisachite choipa pamaso panu. M'dzina la Yesu, Ameni.