Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

NDIME ZA MULUNGU

Mulungu ndi wamphamvuzonse ndipo walonjeza kukhala nawe. Amachita zodabwitsa ndipo amasamalira iwe, ingomukhulupirira. Iye ndi Mpulumutsi wako ndipo ndi chifukwa chake anatumiza Mwana wake wobadwa yekha kuti atiferere machimo ako.

Mwa Mulungu, zonse n’zotheka ngati uli ndi chikhulupiriro. Kuti umudziwe Mulungu, uyenera kuyandikira kwa Iye m’pemphero ndi m’Mawu ake. Ambuye akufuna kuti umuyandikire.

Njira ya Mulungu ndi yangwiro; mawu a Yehova ndi oyesedwa. Iye ndi chishango kwa onse amene amamukhulupirira. (2 Samueli 22:31)


Akolose 3:21

Inu atate, musamaŵapsetsa mtima ana anu, kuti angataye mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
3 Yohane 1:4

Palibe chondikondweretsa kwambiri koposa kumva kuti ana anga akuyenda m'choona.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 23:25

Atate ako ndi amai ako asangalale, mai amene adakubala iwe akondwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:6

Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ulemerero wa ana ndi atate ao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 128:3-4

Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka, m'kati mwa nyuma yako. Ana ako adzakhala ngati tiziphukira taolivi, kuzungulira tebulo lako.

Zoonadi, ndimo m'mene adzakhalire wodala munthu woopa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 127:3-5

Zoonadi, ana ndi mphatso yochokera kwa Chauta, zidzukulu ndi mphotho yake.

Ana apaunyamata ali ngati mivi m'manja mwa munthu wankhondo.

Ngwodala amene phodo lake nlodzaza ndi mivi yotere. Sadzamchititsa manyazi akamalankhula ndi adani ake pa bwalo lamilandu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 23:24

Bambo wa mwana waulemu adzakondwa kwambiri. Wobala mwana wanzeru adzasangalala naye.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:1

Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa atate ake, koma mwana wopusa amanyoza amai ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 6:6-7

Muziŵasunga bwino mumtima mwanu malamulo amene ndikukupatsani leroŵa.

Muziŵaphunzitsa mwachangu kwa ana anu kulikonse kumene muli, mutakhala pansi m'nyumba mwanu, kapena muli paulendo, kapena mukupumula, kapena mukugwira ntchito.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 127:4-5

Ana apaunyamata ali ngati mivi m'manja mwa munthu wankhondo.

Ngwodala amene phodo lake nlodzaza ndi mivi yotere. Sadzamchititsa manyazi akamalankhula ndi adani ake pa bwalo lamilandu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 8:56

Atate anu Abrahamu adaasekera poyembekeza kuti adzaona tsiku la kubwera kwanga. Adaliwonadi nakondwa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yoswa 24:15

Ngati simufuna kutumikira Chauta, sankhani lero lomwe lino amene muti mudzamtumikire, kapena ndi milungu ya Aamori amene mukukhala nawo m'dziko mwao. Koma ine pamodzi ndi banja langa lonse, tidzatumikira Chauta.”

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 9:15

Tiyamike Mulungu chifukwa cha mphatso yake yosaneneka.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 22:6

Mwana muzimuphunzitsa njira yoti aziyendamo, ndipo atakalamba sadzachokamo m'njira imeneyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:13

Monga bambo amachitira chifundo ana ake, ndi momwenso Chauta amaŵachitira chifundo omulemekeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:24

Lero ndiye tsiku limene Chauta adalipanga. Tiyeni tikondwe ndi kusangalala pa tsiku limeneli.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:11-12

Mwana wanga, usanyoze malango a Chauta, usatope nako kudzudzula kwake.

Paja Chauta amadzudzula yemwe amamkonda, monga momwe atate amamchitira mwana wokondwera naye.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:18

Uzimlanga mwana wako chikhulupiriro chikadalipo, ukapanda kutero, wamuwononga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 22:15

Kupusa kumakhala mumtima mwa mwana, koma ndodo yomlangira mwanayo idzachotsa kupusako.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:24

Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti samkonda, koma amene amakonda mwana wake, sazengereza kumlanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 28:7

Amene amatsata malamulo ndiye mwana wanzeru, koma amene amayenda ndi anthu adyera, amachititsa atate ake manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:26

Munthu woopa Chauta ali ndi chikhulupiriro cholimba, ndipo ana ake adzakhala napo pothaŵira.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 29:17

Uzimlanga mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere mu mtima, adzakondweretsa mtima wako m'tsogolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:7

Munthu abwino amakhala mwachilungamo, ndipo Mulungu amadalitsa ana amene amatsata njira yake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 128:1-4

Ngwodala aliyense woopa Chauta, amene amayenda m'njira zake.

Udzadya zimene manja ako adagwirira ntchito. Udzasangalala, ndipo zinthu zidzakuyendera bwino.

Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka, m'kati mwa nyuma yako. Ana ako adzakhala ngati tiziphukira taolivi, kuzungulira tebulo lako.

Zoonadi, ndimo m'mene adzakhalire wodala munthu woopa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 38:19

Amoyo, amoyo okha, ndiwo amakutamandani, monga m'mene ndikuchitira ine tsopanomu. Atate amauza ana ao za kukhulupirika kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mika 6:8

Iyai, Chauta adakuwonetsa kale, munthu iwe, chimene chili chabwino. Zimene akufuna kuti uzichita ndi izi: uzichita zolungama, uzikhala wachifundo, ndipo uziyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:10

Muzikondana kwenikweni monga abale, ndipo muzichita ngati kupikisana poonetsana ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 11:11-13

Ndani mwa atatenu, mwana wake atampempha nsomba, iye nkumupatsa njoka?

Kapena atampempha dzira, iye nkumupatsa chinkhanira?

Tsono ngati inu, nkuipa kwanuku, mumadziŵa kupatsa ana anu mphatso zabwino, nanji Atate akumwamba, angalephere bwanji kupereka Mzimu Woyera kwa amene aŵapempha.”

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:25-28

Inu amuna, muzikonda akazi anu, monga momwe Khristu adakondera Mpingo, nadzipereka chifukwa cha Mpingowo.

Adachita zimenezi kuti aupatule ukhale wakewake, atauyeretsa pakuutsuka ndi madzi ndiponso ndi mau ake.

Adafuna kuti akauimike pamaso pake uli waulemerero, wopanda banga kapena makwinya, kapena kanthu kena kalikonse kouipitsa, koma uli woyera ndi wangwiro kotheratu.

Momwemonso amuna azikonda akazi ao, monga momwe eniakewo amakondera matupi ao. Amene amakonda mkazi wake, ndiye kuti amadzikonda iye yemwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:4

Inu atate, musamaŵapsetsa mtima ana anu, koma muziŵalera bwino pakuŵasungitsa mwambo ndi malangizo a Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 2:11-12

Paja mukudziŵa kuti, tinkasamala aliyense mwa inu monga momwe amachitira bambo ndi ana ake.

Tinkakulimbitsani mtima, kukuthuzitsani mtima ndi kukupemphani kuti mayendedwe anu akhale okomera Mulungu, amene amakuitanani kuti mukaloŵe mu Ufumu wake waulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 5:8

Ngati wina aliyense saŵapatsa zofunika achibale ake, makamaka a m'banja mwake momwe, ameneyo wataya chikhulupiriro chake, ndipo kuipa kwake nkoposa kwa munthu wosakhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:7-9

Muzipirira masautso kuti muphunzirepo makhalidwe oyenera. Mulungu amakutengani ngati ana ake m'zochita zake zonse. Kodi nkale lonse analipo mwana amene bambo wake sadamlange?

Ngati Mulungu sakulangani inuyo, monga amachitira ndi ana ake onse, ndiye kuti sindinu ana enieni, koma am'chigololo.

Tinali nawo azibambo athu apansipano amene ankatilanga, ndipo tinkaŵalemekeza. Kwenikweni tsono tikadayenera kugonjera Mulungu, Atate a mizimu, kuti tikhale ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:5

Wina mwa inu akasoŵa nzeru, apemphe kwa Mulungu, ndipo adzalandira, pakuti Mulungu amapereka kwa onse mwaufulu ndi mosatonzera.

Mutu    |  Mabaibulo