Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -


111 Mau a m'Baibulo Okhudza Chilengedwe

111 Mau a m'Baibulo Okhudza Chilengedwe

Ndikayang'ana chilengedwe cha Mulungu, kukongola kwake konse, ndimadabwa kwambiri ndi ukulu wake ndi dongosolo lake labwino. Kuyambira kale, anthufe timayesetsa kumvetsa dziko ndi cholinga chake m'njira zosiyanasiyana. Koma Baibulo limatipatsa njira yoona zinthu yotithandiza kumvetsa bwino dzikoli.

M'mavesi oyamba a buku la Genesis, timapeza kuti Mulungu ndiye analenga thambo ndi dziko lapansi, ndi zonse zili mmenemo. "Pachiyambi Mulungu analenga thambo ndi dziko lapansi." (Genesis 1:1). Mawu awa, ochepa koma ofunika kwambiri, amatiuza kuti chilengedwe chonse chinachokera kwa Mulungu. Dziko linapangidwa ndi Mlengi Wamkulu.

Baibulo limatilimbikitsa kuona kupitirira zomwe maso athu akuona, ndikuganizira cholinga chenicheni cha chilengedwechi. Mu Salmo 19:1, limati: "Zakumwamba zimalengeza ulemerero wa Mulungu; ndipo thambo limasonyeza ntchito ya manja ake." Apa tikuona kuti dziko sili mboni chete ya ukulu wa Mulungu, koma limalankhulanso za kukhalapo ndi mphamvu zake kwa ife.

Dziko limatilimbikitsa kuona ukulu wa Mulungu m'chilengedwe chake. Limatithandiza kumvetsa kuti dziko limene tikukhala ndilo umboni wa chikondi, mphamvu, ndi nzeru za Mlengi wathu.




Ahebri 11:3

Pokhala ndi chikhulupiriro timamvetsa kuti zonse zimene zilipo zidalengedwa ndi mau a Mulungu, mwakuti zinthu zoonekazi zidachokera ku zinthu zosaoneka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 1:1

Pachiyambi Mulungu adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 115:15

Akudalitseni Chauta, amene adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 4:11

“Inu Ambuye athu ndi Mulungu wathu, ndinu oyenera kulandira ulemerero, ulemu ndi mphamvu, pakuti ndinu mudalenga zinthu zonse. Mudafuna kuti zonsezo zikhalepo, ndipo zidalengedwa.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 19:1

Zakumwamba zimalalika ulemerero wa Mulungu, thambo limasonyeza ntchito za manja ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 14:19

Adadalitsa Abramuyo, adati, “Mulungu Wopambanazonse, Mlengi wa kumwamba ndi dziko lapansi, akudalitse iwe Abramu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mafumu 19:15

Tsono adapemphera kwa Chauta kuti, “Inu Chauta, Mulungu wa Israele, amene mumakhala pa mpando wanu waufumu pamwamba pa akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira mafumu onse a dziko lonse lapansi. Mudalenga dziko lakumwamba ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 37:16

“Inu Chauta Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israele, amene mumakhala pa mpando wanu waufumu pamwamba pa akerubi, inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lonse lapansi. Mudalenga dziko lakumwamba ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 44:24

Chauta, Mpulumutsi wako, amene adakupanga m'mimba mwa mai wako, akunena kuti, “Ndine Chauta, amene ndidapanga zinthu zonse. Pamene ndinkayalika zakuthambo, ndinali ndekha. Pamene ndinkalenga dziko lapansi, kodi analipo amene adandithandiza?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:16

Kudzera mwa Iye Mulungu adalenga zonse zakumwamba ndi zapansipano, zooneka ndi zosaoneka, mafumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu ena onse. Mulungu adalenga zonse kudzera mwa Iye, zonsezo adalengera Iyeyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 26:7

Mulungu adayala thambo lakumpoto pa phompho, adakoloŵeka dziko lapansi m'malo mwake, pamene panali popanda nkanthu komwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 33:25

Koma Ine Chauta ndidachita chipangano ndi usana ndi usiku, ndipo ndidapanga malamulo oyendetsa zonse za pa dziko lapansi ndi zamumlengalenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:6

Chauta adalankhula ndipo zakumwamba zidalengedwa. Zonse zakumeneko zidalengedwa pamene Iye adalankhula mau ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 11:25

Pa nthaŵi imeneyo Yesu adati, “Atate, Mwini kumwamba ndi dziko lapansi, ndikukuyamikani kuti zinthuzi mudaululira anthu osaphunzira, nkubisira anthu anzeru ndi ophunzira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:3

Mulungu adalenga zonse kudzera mwa Iye, ndipo palibe chilichonse chimene chidalengedwa popanda Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 32:17

“Ha! Inu Chauta! Mudalenga ndinu dziko lakumwamba ndi dziko lapansi. Mudazilenga ndi dzanja lanu lamphamvu kwambiri. Palibe chokukanikani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 9:6

Pamenepo Ezara adapemphera kuti, “Inu nokha ndiye Chauta. Inu mudalenga kumwamba, kumwambamwamba, ndiponso zonse zokhala komweko, dziko lapansi ndi zonse zokhala m'menemo. Mudalenga nyanja ndi zonse zam'menemo. Zonse zakumwamba zimakupembedzani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 45:12

Ndine amene ndidalenga dziko lapansi ndi kulenga munthu kuti akhalemo. Ndidayalika zakuthambo ndi manja anga, ndipo tsopano ndimalamulira gulu lonse lamumlengalenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:4

Amadziŵa chiŵerengero cha nyenyezi, zonse amazitcha maina ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 4:13

Tsono tamvani, Iyeyo ndiye amene amaumba mapiri ndi kupanga mphepo, ndiye amene amaululira munthu za m'maganizo mwake, ndiye amene amasandutsa usana kuti ukhale usiku, ndiye amene amayenda pa zitunda za dziko lapansi. Dzina lake ndi Chauta, Mulungu Wamphamvuzonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 10:12

Chauta ndiye amene adalenga dziko lapansi ndi mphamvu zake. Ndiye amene adapanga zonse ndi nzeru zake ndipo ndi umisiri wake adayala thambo lakumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 38:4-7

“Kodi udaali kuti pamene ndinkaika maziko a dziko lapansi? Undiwuze ngati ndiwe womvetsa zinthu. pamene ili khale m'mapanga mwake, kapena pamene ikubisala m'tchire? Kodi khwangwala amampatsa chakudya chake ndani, pamene maunda ake akulirira kwa Mulungu, namadzandira chifukwa chosoŵa chakudya?” Nanga kodi ukudziŵa amene adalemba malire ake, amene adayesapo ndi chingwe padzikopo? Kodi maziko ake adaŵakumba potani? Nanga mwala wake wapangodya adauika ndani? Pa nthaŵiyo nyenyezi zakuvuma zinkaimba pamodzi, ndipo angelo onse a Mulungu ankafuula mokondwa?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 8:3-4

Ndikamayang'ana ku thambo lanu limene mudapanga ndi manja anu, ndikamaona mwezi ndi nyenyezi zimene mudazikhazika kumeneko, ndimadzifunsa kuti, “Kodi munthu nchiyani kuti muzimkumbukira, mwana wa munthu nchiyani kuti muzimsamalira?”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 42:5

Mulungu, Chauta, adalenga zakuthambo ndi kuziyalika. Adalenga dziko lapansi ndi zonse zimene limabereka. Adapatsa mpweya kwa anthu okhala m'dzikomo, ndi kuninkha moyo kwa onse oyendamo. Iyeyo akunena kuti,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:5

Mudakhazika dziko lapansi pa maziko ake, kuti lisagwedezeke konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:26

Yang'anani kumlengalenga. Kodi ndani adalenga nyenyezi mukuziwonazi? Ndiye amene amazitsogolera ngati gulu lankhondo, ndipo iliyonse amaiitana ndi dzina lake. Popeza kuti nyonga ndi mphamvu zake nzazikulu. Palibe ndi imodzi yomwe imene imasoŵapo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 1:14-18

Pambuyo pake Mulungu adati, “Kuthambo kukhale miyuni kuti izilekanitsa usana ndi usiku, ndiponso kuti ikhale zizindikiro za nyengo, masiku ndi zaka. Miyuni imeneyi ikhale ku thambo ndi kumaunikira dziko lapansi,” ndipo zidachitikadi. Motero Mulungu adalenga miyuni iŵiri yaikulu: dzuŵa loŵala masana, ndi mwezi woŵala usiku. Adalenganso nyenyezi. Mulungu adaika miyuniyo ku thambo, kuti iziwunikira dziko lapansi, kuti iziŵala usana ndi usiku, kulekanitsa kuyera ndi mdima. Mulungu adaona kuti zinali zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 2:1

Motero dziko lonse lapansi, thambo ndi zonse zokhala m'menemo, zidatha kulengedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 136:5-9

Adalenga zakumwamba ndi nzeru zake, pakuti chikondi chake nchamuyaya. Adayala dziko lapansi pa madzi, pakuti chikondi chake nchamuyaya. Adalenga miyuni yaikulu yamumlengalenga, pakuti chikondi chake nchamuyaya. Dzuŵa kuti lizilamulira usana, pakuti chikondi chake nchamuyaya. Mwezi ndi nyenyezi kuti zizilamulira usiku, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 10:14

Kumwamba ndi zonse zili kumeneko ndi zake za Chauta, pamodzi ndi dziko lapansi pano ndi zonse zili m'menemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 89:5

Zakumwamba zimatamanda zodabwitsa zanu, Inu Chauta, zimatamanda kukhulupirika kwanu mu msonkhano wa oyera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 5:8

Iye uja ndiye amene adalenga nyenyezi za Akamwiniatsatana ndiponso Nsangwe, ndiye amene amasandutsa mdima kuti ukhale m'maŵa nasandutsa usana kuti ukhale usiku. Ndiye amene amaitana madzi am'nyanja ndi kuŵathira pa dziko lapansi. Dzina lake ndi Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 136:5

Adalenga zakumwamba ndi nzeru zake, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:2

Mumadzifunditsa ndi kuŵala ngati chovala, mwatambasula mlengalenga ngati hema.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:19-20

Pamene adakhazikitsa dziko lapansi, Chauta adaonetsa nzeru. Pamene adakhazikitsa zakumwamba, adaonetsa nzeru za kumvetsa bwino. Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka, ndipo udzakhala ndi moyo wabwino kwambiri. Pamene adatumphutsa madzi kuchoka kunsi kwa dziko, ndipo mitambo idagwetsa mvula, adaonetsa nzeru zodziŵa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 48:13

Manja anga adamanga maziko a dziko lapansi, dzanja langa lamanja lidafunyulula mlengalenga. Ndikaitana dziko lapansi ndi dziko lakumwamba, zonsezo zimabwera pamodzi kwa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 148:3

Mtamandeni inu dzuŵa ndi mwezi, mtamandeni inu nonse nyenyezi zoŵala!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:19

Pamene adakhazikitsa dziko lapansi, Chauta adaonetsa nzeru. Pamene adakhazikitsa zakumwamba, adaonetsa nzeru za kumvetsa bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 9:8

Ndi Mulungu yekha amene adayala zakuthambo, ndiye amayenda pa mafunde apanyanja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 89:11

Zakumwamba ndi zanu, dziko lapansi nalonso ndi lanu. Mudapanga dziko lonse ndi zonse zam'menemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 115:16

Kumwamba nkwa Chauta, koma dziko lapansi adapatsa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:3

Iye ndiye kuŵala koonetsa ulemerero wa Mulungu, ndipo ndiye chithunzi chenicheni chosonyeza khalidwe la Mulungu. Iyeyu amachirikiza zonse ndi mau ake amphamvu. Atayeretsa mtundu wa anthu pakuŵachotsa machimo, adakakhala Kumwamba, ku dzanja lamanja la Mulungu waulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 102:25-27

Inu mudaika maziko a dziko lapansi kalekale, ndipo zakumwamba mudazipanga ndi manja anu. Zonsezi zidzatha ngati malaya, koma Inu mulipobe. Inu mumazisintha ngati chovala, ndipo zimatha. Koma Inu simusintha, zaka zanu sizitha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:22

Dziko lapansi lidalengedwa ndi Iye amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba, kuseri kwa mlengalenga. Amaona anthu pansi ngati ziwala. Adafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchingira, ngati hema lokhalamo anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:20

Pajatu chilengedwere cha dziko lapansi anthu akhala akuzindikira makhalidwe osaoneka a Mulungu, ndiye kuti mphamvu zake zosatha, ndiponso umulungu wake. Akhala akuzizindikira poona zimene Mulungu adalenga. Choncho alibe konse pozembera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 3:11

Adapanga chinthu chilichonse kuti chikhale chabwino pa nthaŵi yake. M'mitima mwa anthu Mulungu adaikanso nzeru zotanthauzira zochitika za pa mibadwo ndi mibadwo. Komabe anthuwo sangathe kuzitulukira ntchito zonse za Mulungu kuyambira pa chiyambi mpaka pomalizira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 148:3-5

Mtamandeni inu dzuŵa ndi mwezi, mtamandeni inu nonse nyenyezi zoŵala! Mtamandeni inu thambo lakumwambamwamba, ndi inu madzi a pamwamba pa thambo! Zonsezo zitamande dzina la Chauta! Paja Iye adaalamula, izo nkulengedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 24:1-2

Dziko lapansi ndi zonse zam'menemo ndi za Chauta, dziko lonse lapansi pamodzi ndi anthu onse okhalamo ndi ake. Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Ndi Chauta Wamphamvuzonse. Iyeyo ndiye Mfumu yaulemerero. Pakuti iye ndi amene adaika dziko lapansi pa nyanja yaikulu, adalikhazika pa mitsinje yozama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:17

Iyeyo analipo zinthu zonse pakadalibe, mwa Iye zinthu zonse zimalunzana pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:9

Monga momwe mlengalenga uliri kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 90:2

Mapiri asanabadwe, ndipo musanalenge dziko lapansi ndi pokhala anthu, ndinu Mulungu kuyambira muyaya mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 26:14

Zimenezi ndi pang'ono chabe za makhalidwe ake. Tingomva pang'ono za Iye ngati kunong'ona. Koma ndani angadziŵe kukula kwa mphamvu zake?”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:5

Ndidzasinkhasinkha za ulemerero ndi za ufumu wanu waukulu, ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 93:1

Chauta ndiye mfumu. Wavala ulemerero, wavala mphamvu ngati lamba. Iye adakhazikitsa dziko lapansi, silidzagwedezeka konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 3:4

Nyumba iliyonse imamangidwa ndi munthu wakutiwakuti, koma amene adapanga zonse, ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 16:26

Paja milungu ya anthu a mitundu ina ndi mafano chabe, koma Chauta ndiye adalenga zakumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 65:17

Chauta akunena kuti, “Ndikulenga thambo lam'mwamba latsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zakale sadzazikumbukiranso, zidzaiŵalika kotheratu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:24-25

Inu Chauta ntchito zanu nzambiri, zonse mwazipanga mwanzeru, ndipo dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu. Kuli nyanja yaikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zinthu zosaŵerengeka, zinthu zamoyo, zazing'ono ndi zazikulu zomwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:12

Kodi ndani adayesa kuchuluka kwa madzi am'nyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyesa kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani adayesa dothi lonse la dziko lapansi ndi dengu? Ndani adayesa kulemera kwa mapiri ndi magomo pa sikelo?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 22:12

“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ona nyenyezi zili m'mwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene ziliripo!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 148:1-6

Tamandani Chauta! Tamandani Chauta inu okhala kumwamba, mtamandeni inu okhala mu mlengalenga! Inu nyama zakutchire ndi zoŵeta zonse, inu zinthu zokwaŵa ndi mbalame zouluka! Inu mafumu a pa dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse, inu akuluakulu ndi olamulira dziko lapansi! Inu anyamata pamodzi ndi anamwali, inu nkhalamba ndi ana omwe! Onsewo atamande dzina la Chauta, pakuti dzina lake lokha nlolemekezeka, ulemerero wake ndi woposa, pansi pano nkumwamba komwe. Chauta wakweza anthu ake poŵapatsa mphamvu. Walemekeza anthu ake onse oyera mtima, Aisraele amene Iye amaŵakonda. Tamandani Chauta! Mtamandeni inu angelo ake onse, mtamandeni inu magulu a ankhondo ake onse! Mtamandeni inu dzuŵa ndi mwezi, mtamandeni inu nonse nyenyezi zoŵala! Mtamandeni inu thambo lakumwambamwamba, ndi inu madzi a pamwamba pa thambo! Zonsezo zitamande dzina la Chauta! Paja Iye adaalamula, izo nkulengedwa. Adazikhazikitsa kuti zikhale mpaka muyaya, adaikapo lamulo limene silingathe kusinthika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 96:5

Paja milungu yonse ya mitundu ina ya anthu ndi mafano chabe. Koma Chauta ndiye adalenga zakumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 8:6

Koma kwa ife, Mulungu ndi mmodzi yekha, ndiye Atate, amene adalenga zonse, ndipo moyo wathu umalinga kwa Iye. Tilinso ndi Ambuye amodzi okha, Yesu Khristu. Mulungu adalenga zonse kudzera mwa Iye, ndipo ife tili ndi moyo chifukwa cha Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 10:12-13

Chauta ndiye amene adalenga dziko lapansi ndi mphamvu zake. Ndiye amene adapanga zonse ndi nzeru zake ndipo ndi umisiri wake adayala thambo lakumwamba. Iye akalankhula, kumamveka mkokomo wa madzi kumwamba, ndiye amene amadzetsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amang'animitsa mphezi za mvula, amakunthitsa mphepo kuchokera kumene amaisunga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 21:1

Pambuyo pake ndidaona thambo latsopano ndi dziko lapansi latsopano. Paja thambo loyamba lija ndi dziko lapansi loyamba lija zinali zitazimirira, ndipo nyanja panalibenso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 74:16-17

Mudalenga usana ndi usiku. Mudaika mwezi ndi dzuŵa m'malo mwake. Mudalemba malire a dziko lapansi, mudakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:11

Paja pa masiku asanu ndi limodzi Chauta adalenga zonse zakumwamba, za pa dziko lapansi, nyanja ndi zinthu zonse zam'menemo, koma pa tsiku lachisanu ndi chiŵiri adapumula. Nchifukwa chake Chauta adadalitsa tsiku la Sabata, nalisandutsa loyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:19

Inu mudapanga mwezi kuti uzisiyanitsa nyengo, ndipo dzuŵa limadziŵa nthaŵi yake yoloŵera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 45:18

Akutero Chauta amene adalenga zakumwamba, ndi Iyeyo Mulungu amene adaumba ndi kulenga dziko lapansi, ndipo adalikhazikitsa mwamphamvu. Sadalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma kuti likhale malo okhalamo anthu. Iyeyo akunena kuti: “Chauta ndine, palibenso wina ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:9

pakuti Iye adalankhula, ndipo zidachitikadi, adalamula, ndipo zidaonekadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 51:13

Kodi ndinu yani kuti muziiŵala Chauta, Mlengi wanu, amene adayalika zakuthambo, ndi kuika maziko a dziko lapansi? Kodi ndinu yani kuti nthaŵi zonse muziwopa ukali wa anthu okuzunzani, amene angofuna kukuwonongani? Ukali wa anthu okuzunzaniwo tsopano uli kuti?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 1:31

Mulungu adaona kuti zonse zimene adalengazo zinali zabwino kwambiri. Tsono kudali madzulo ndiponso m'maŵa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 37:14-16

“Inu aYobe, tamvani izi, imani, muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu. Kodi mukudziŵa m'mene Mulungu amazichitira, ndi m'mene amang'anipitsira mphezi m'mitambo yake? Kaya mukudziŵa m'mene Mulungu amayalira mitambo, ntchito yosonyeza nzeru zake zodabwitsa,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 66:1-2

Chauta akunena kuti, “Thambo lam'mwamba ndiye mpando wanga waufumu, dziko lapansi ndiye chopondapo mapazi anga. Kodi ndi nyumba yotani imene mungathe kundimangira inu? Ndi malo otani amene inu mungandikonzere kuti Ine ndizipumulirapo? “Kondwera nayeni Yerusalemu, musangalale chifukwa cha iye, inu nonse amene mumakonda mzinda umenewu. Kondwera nayeni mwachimwemwe, nonsenu amene mukumlira. Mudzalandira chitonthozo ndi kukondwera nacho kwambiri. Mudzagaŵana naye ulemerero wake ndi kusangalala nawo.” Chauta akunena kuti, “Ndidzakupatsa zabwino zochuluka ngati mtsinje wa madzi. Chuma cha mitundu ya anthu chidzafika kwa inu ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene mai wake wamnyamulira pambalipa, kapena akumluluza pa maondo. Ndidzakusangalatsani ku Yerusalemu monga momwe mai amasangalatsira mwana wake. Mudzasangalala poona zimenezi. Zidzakulimbitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Tsono mudzadziŵa kuti Ine Chauta ndimathandiza amene amandimvera, ndipo ndimakwiyira adani anga.” “Pajatu Chauta adzabwera ndi moto. Ndipo magaleta ake adzafika ngati mkuntho. Iye adzaonetsa poyera ukali wake, ndipo adzalanga adani ake ndi malaŵi a moto. Adzalanga anthu onse a pa dziko lapansi ndi moto ndi lupanga. Alipo ambiri amene Chauta adzaŵapha.” Chauta akunena kuti, “Amene akuti akudzipatula ndi kudziyeretsa pamene akufuna kuchita miyambo yam'minda ija, ali ndi mtsogoleri wao yemwe, nkumadya nyama yankhumba, mbeŵa ndi zonyansa zina, onsewo adzafera limodzi,” akuterotu Chauta. “Ndikudziŵa ntchito zao ndi maganizo ao. Ndikubwera kudzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndi a zilankhulo zonse. Adzabweradi ndipo adzaona ulemerero wanga. “Ndidzaika chizindikiro pakati pao. Mwa iwowo padzakhala ena opulumukako amene ndidzaŵatuma kwa anthu a mitundu ina, monga a ku Tarisisi, a ku Puti ndi a ku Ludi, akatswiri a mauta, ndiponso ku Tubala, ku Yavani, ndi ku maiko akutali amene sadamvepo za mbiri yanga kapena kuwona ulemerero wanga. Iwowo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina. Zinthu zonsezi ndidazilenga ndine, tsono zonsezi nzanga,” akutero Chauta. “Anthu amene ndimakondwera nawo ndi aŵa: odzichepetsa ndi olapa, ondiwopa ndi omvera mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 2:10

Paja Mulungu amene ndi Mlengi wa zonse ndipo zonse zimalinga kwa Iye, adafuna kufikitsa ana ake ambiri ku ulemerero. Tsono kudaamuyenera kuti mwa njira ya zoŵaŵa, amsandutse Yesu mtsogoleri wangwiro woŵatsogolera ku chipulumutso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 97:6

Zakumwamba zimalalika za kulungama kwake, ndipo anthu a mitundu yonse amaona ulemerero wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:15

Mitundu ya anthu ili ngati kadontho ka madzi mu mtsuko, ilinso ngati fumbi chabe pa sikelo. M'manja mwa Chauta zilumba nzopepuka ngati fumbi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:1-2

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga. Inu Chauta, Mulungu wanga, ndinu aakulu kwambiri. Mumavala ulemu ndi ufumu. Inu mumatumphutsa akasupe m'zigwa, mitsinje imayenda pakati pa mapiri. Imapatsa nyama zonse zakuthengo madzi akumwa, mbidzi zimapherapo ludzu. Mbalame zimamanga zisa pafupi ndi mitsinjeyo, zimaimba m'nthambi za mitengo. Inu mumathirira mapiri ndi madzi ochokera ku malo anu akumwamba. Dziko lapansi ladzaza ndi madalitso anu. Mumameretsa udzu kuti ng'ombe zidye, ndi zomera kuti munthu azilima ndi kupeza chakudya m'nthaka. Amapezamo vinyo wosangalatsa mtima wake, mafuta odzola kuti thupi lake lisisire, ndiponso buledi kuti ampatse mphamvu. Mitengo ya Chauta amaithirira ndi madzi ambiri, mikungudza ya ku Lebanoni imene adaibzala. Mbalame zimamanga zisa m'menemo, dokowe amamanga chisa m'mikungudzamo. M'mapiri aatali ndimo m'mene mumakhala mbalale, m'matanthwe ndimo m'mene mumathaŵira mbira. Inu mudapanga mwezi kuti uzisiyanitsa nyengo, ndipo dzuŵa limadziŵa nthaŵi yake yoloŵera. Mumadzifunditsa ndi kuŵala ngati chovala, mwatambasula mlengalenga ngati hema.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:30

Mukatumiza mpweya wanu zimalengedwa, ndipo mumakonzanso maonekedwe a dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 17:24

“Atate, ndifuna kuti amene mudandipatsa, iwonso akhale pamodzi ndi Ine kumene ndili. Ndifuna kuti aone ulemerero wanga umene mudandipatsa, chifukwa mudandikonda dziko lapansi lisanalengedwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 8:27-29

Ine ndinalipo kale, pamene ankakhazikitsa zakumwamba, pamene ankalemba mzere wa malire a nyanja yozama, pamene ankaika thambo m'malo mwake, pamene ankatsekula akasupe a m'nyanja yozama, pamene ankaika malire a nyanja kuti madzi ake asabzole malirewo, pamene ankaika maziko a dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Petro 3:5

Apa akuiŵala dala kuti kalelo Mulungu atanena mau, zakuthambo zidalengedwa, ndipo dziko lapansi lidapangidwa ndi madzi kufumira m'madzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 26:10

Madzi Mulungu adaŵalembera malire onga uta, motero adalekanitsa kuŵala ndi mdima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 9:6

Ndiwo amene amamanga malo ao okhalamo kumwamba, naika thambo ngati denga la dziko lapansi, amaitana madzi akunyanja naŵakhuthulira pa dziko lapansi. Iwowo dzina lao ndi Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:13-14

Inu mumathirira mapiri ndi madzi ochokera ku malo anu akumwamba. Dziko lapansi ladzaza ndi madalitso anu. Mumameretsa udzu kuti ng'ombe zidye, ndi zomera kuti munthu azilima ndi kupeza chakudya m'nthaka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 45:8

“Gwetsa mvula, iwe thambo, kuchokera kumwamba, mitambo ikhuthule chilungamo chopulumutsa. Dziko lapansi litsekuke kuti patuluke chipulumutso, kuti chilungamo chimerepo. Ndine, Chauta, amene ndidalenga zimenezi.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:28

Kodi sudziŵa? Kodi sudamve? Chauta ndiye Mulungu wachikhalire, Mlengi wa dziko lonse lapansi. Satopa kapena kufooka, palibe amene amadziŵa maganizo ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 10:6

Atatero adalumbira m'dzina la Mulungu wokhala ndi moyo mpaka muyaya, amene adalenga thambo lakumwamba ndi zonse zokhala kumeneko, dziko lapansi ndi zonse zokhala m'menemo, ndiponso nyanja ndi zonse zokhala m'menemo. Mngeloyo kulumbira kwake adati, “Pasakhalenso zochedwa tsopano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 5:9

Ntchito zake ndi zazikulu ndi zosamvetseka. Zodabwitsa zimene amachita ndi zosaŵerengeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:14

Ndikukutamandani, Inu oopsa ndi odabwitsa. Ntchito zanu zonse nzodabwitsa. Mumandidziŵa bwino kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:4

Chauta adapanga chinthu chilichonse kuti chikhale ndi cholinga chake, ngakhale anthu oipa, kuti aone tsiku la mavuto.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 43:7

Onsewo amadziŵika ndi dzina langa, ndidaŵalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndidaŵapanga ndi kuŵapatsa moyo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 1:26-28

Pamwamba pa thambo lija panali chinthu china chooneka ngati mpando waufumu, wopangidwa ndi mwala wa safiro. Pamwamba pa mpandowo panali chinthu chooneka ngati munthu. M'mwamba mwa chiwuno chake munali ngati chitsulo choŵala konsekonse ngati moto. M'munsi mwa chiwuno chake munalinso ngati moto wokhawokhawo. Kuŵala kwamphamvu kudaamzungulira munthuyo. Kuŵalako kunali ndi maonekedwe a utawaleza m'mitambo tsiku limene kwagwa mvula. Umu ndi m'mene ulemerero wa Chauta unkaonekera. Ndidangoti ntauwona, ndidadzigwetsa pansi chafufumimba, ndipo ndidamva mau ondilankhula.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 136:7-9

Adalenga miyuni yaikulu yamumlengalenga, pakuti chikondi chake nchamuyaya. Dzuŵa kuti lizilamulira usana, pakuti chikondi chake nchamuyaya. Mwezi ndi nyenyezi kuti zizilamulira usiku, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 14:7

Mngeloyo adanena mokweza mau kuti, “Opani Mulungu ndi kumtamanda, pakuti yafika nthaŵi yoti aweruze anthu. Mumpembedze Iye amene adalenga thambo, dziko lapansi, nyanja, ndi akasupe a madzi.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 15:11

“Inu Chauta, kodi pali mulungu wina wofanafana nanu? Ndani amafanafana ndi Inu, amene muli aulemu chifukwa cha ungwiro wanu? Ndani amafanafana nanu, Inu amene muli oopsa chifukwa cha ntchito zanu zaulemu ndi zodabwitsa?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 9:9

Ndiye amene adalenga nyenyezi za Mlalang'amba ndi Akamwiniatsatana, Nsangwe ndi Kumpotosimpita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:31-32

Ulemerero wa Chauta ukhalebe mpaka muyaya, Chauta akondwe nazo ntchito zakezo, Iye amati akayang'ana dziko lapansi, limanjenjemera, akakhudza mapiri, mapiriwo amafuka nthunzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:90-91

Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka pa mibadwo yonse. Inu mwakhazikitsa dziko, ndipo siligwedezeka. Zolengedwa zikupezeka lero lino chifukwa cha kulamula kwanu, pakuti zinthu zonse zimakutumikirani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 26:8

Amasunga madzi ambiri m'mitambo yochindikira, koma mitamboyo sing'ambika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 1:27

Motero Mulungu adalenga munthu, m'chifanizo chake, adaŵalengadi m'chifanizo cha Mulungu. Adaŵalenga wina wamwamuna wina wamkazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:5

Mbuye wathu ndi wamkulu, ndipo ndi wa mphamvu zambiri, nzeru zake nzopanda malire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 111:2-3

Ntchito za Chauta nzazikulu, onse okondwera nazo amazilingalira. Ntchito zake ndi zaulemu ndi zaufumu, ndipo kulungama kwake nkwamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:8

Udzu umauma, maluŵa amafota, koma mau a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:10

Wotchedwa Mauyo anali m'dziko lapansi, ndipo Mulungu adalenga dziko lapansilo kudzera mwa Iye, komabe anthu apansipano sadamzindikire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 2:8

Amakweza osauka kuŵachotsa pa fumbi, amachotsa anthu osoŵa pa dzala, amaŵakhazika pamodzi ndi akalonga, amaŵapatsa mpando waulemu. Nsanamira za dziko lapansi nzake za Chauta, adakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:38-39

Ndithu ndikudziŵa mosakayika konse kuti palibe kanthu kangatilekanitse ndi chikondi chake. Ngakhale imfa kapena moyo, ngakhale angelo kapena olamulira, ngakhale zinthu zimene zilipo tsopano, kapena zimene zidzaoneke m'tsogolomo, kapena zamphamvu zina zilizonse, ngakhale zakumwamba kapena zapansi, kapenanso kanthu kena kalikonse kolengedwa, sikangadzatilekanitse ndi chikondi cha Mulungu, chimene tili nacho mwa Khristu Yesu Ambuye athu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:31

Koma amene amakhulupirira Chauta adzalandira mphamvu zatsopano, adzauluka ngati ziwombankhanga. Adzathamanga koma osatopa, adzayenda koma osalefuka konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu wanga, zikomo kwambiri chifukwa cha nzeru zanu zopanda malire ndi mtima wanu wabwino. Ndinu woyenera ulemerero wonse ndi kukwezedwa. Ndikulambirani kuchokera pansi pa mtima wanga, ndinu wangwiro pa zonse zomwe mumachita. Ndikukuthokozani chifukwa cha mphatso yosayerekezeka ya chilengedwe chonse. Nyengozi iliyonse yowala kumwamba, phiri lililonse lalitali, ndi cholengedwa chilichonse chamoyo padziko lapansi ndi umboni wa ukulu wanu. Zikomo Ambuye, chifukwa cha mgwirizano womwe uli m'chilengedwe chonse, chifukwa cha nyimbo yokondweretsa ya dziko lathu. Chikondi chanu ndi chisamaliro chanu zili paliponse m'chilengedwechi, zikutikumbutsa nthawi zonse mphamvu zanu ndi chikondi chanu chosatha. Tikugwada pamaso panu ndi kukuthokozani chifukwa cha moyo umene mwatipatsa. Sindingaleke kukukondani, mwakhala wabwino kwa ine ndi kundizungulira ndi chisomo chanu ndi chiyanjo chanu. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa