Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -


102 Mau a m'Baibulo Okhudza Nsembe

102 Mau a m'Baibulo Okhudza Nsembe

Nsembe ndi mphatso yopatulika kwa Mulungu, yodziwika ndi kumvera, khama, ndi kudzipereka, ndi chiyembekezo cholandira madalitso. Ndi kupereka kwa Ambuye chilichonse chimene akufuna popanda kumukana chilichonse, kumvera malamulo ake mosazengereza ndipo popanda kufuna mafotokozedwe.

Mwa Yesu tikuona chitsanzo chabwino cha izi: Mulungu anafuna kubwezeretsa mtendere pakati pa dziko lapansi ndi Iye, chifukwa tchimo linkatilepheretsa kukhala mu ulemerero wake, koma nsembe ya Yesu imatipatsa mwayi wopembedza Atate wathu wakumwamba mwaufulu. Nsembe zimene umapereka m'moyo wako nthawi zonse zimakupatsa cholinga, ndipo n’chifukwa chake umazichita mwachangu, ukuyembekezera kuona zotsatira zake.

Ambuye wathu sanasamale za ululu umene ankamva; cholinga chake chokha chinali kuchita chifuniro cha Atate wake padziko lapansi. Mulungu anapereka Mwana wake kuti tisatayike, ndiye, kodi iwe uli wokonzeka kupereka chiyani kwa Mulungu?

Akakupempha chinachake, uyenera kukhala wokonzeka kuvomereza popanda kukaikira mavuto amene amabwera chifukwa chomvera malamulo ake, potero kusonyeza chikondi chenicheni chomwe chingakupangitse kusiya dyera, kudzikuza, ndi kufuna kutchuka kwa anthu. Nsembe zimene umapereka si zongofuna kusonyeza anthu ena, koma ndi zochita zachikondi kwa Mlengi wako. Usakane kupereka nthawi yako, ndalama zako, kapena banja lako, chifukwa ngakhale kachitidwe kakang'ono kangayambitse zinthu zazikulu.

Mulungu anapereka moyo wa Mwana wake kuti atipulumutse, ndipo ndi nsembe zathu, masiku ano anthu ambiri akupulumutsidwa ku gehena. Ngakhale nthawi zina nsembe ingakhale yowawa, khala ndi chikhulupiriro kuti Mzimu Woyera adzakuthandiza nthawi zonse ndipo sadzakusiya.




Eksodo 20:24

Mundimangire guwa ladothi, ndipo pamenepo muziperekapo nsembe zanu zopsereza, ndi zopereka zanu zamtendere, nkhosa ndi ng'ombe zanu. Pa malo onse amene ndikuuzani kuti muzindipembedzerapo, Ine ndidzabwera kudzakudalitsani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 1:3-4

“Ngati munthu apereka nsembe yopsereza kwathunthu, azipereka ng'ombe yamphongo yopanda chilema. Aziiperekera pa khomo la chihema chamsonkhano, kuti Chauta ailandire. Tsono asanjike dzanja lake pamutu pa ng'ombeyo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:17

Nsembe imene Inu Mulungu mumailandira, ndi mtima wotswanyika. Mtima wachisoni ndi wolapa, Inu Mulungu simudzaunyoza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:1

Tsono abale, popeza kuti Mulungu watichitira chifundo chachikulu chotere, ndikukupemphani kuti mupereke matupi anu omwe kuti akhale nsembe yamoyo, yopatulika, ndi yokondwetsa Mulungu. Imeneyi ikhale njira yanu yopembedzera Mulungu mwauzimu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 9:22

Malinga ndi Malamulo a Mosewo pafupifupi zonse zimayeretsedwa ndi magazi, ndipo machimo sakhululukidwa popanda kukhetsa magazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:5

Koma adambaya chifukwa cha machimo athu, ndipo adamtswanya chifukwa cha zoipa zathu. Chilango chimene chidamgwera iye chatipatsa ife mtendere, ndipo mabala ake atichiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:20

Ndidapachikidwa pa mtanda pamodzi ndi Khristu, kotero kuti sindinenso amene ndili ndi moyo, koma ndi Khristu amene ali ndi moyo mwa ine. Moyo umene ndili nawo tsopano m'thupi lino, ndi moyo wokhulupirira Mwana wa Mulungu, amene adandikonda napereka moyo wake chifukwa cha ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:17

Ndipotu mwina mwake ndidzaphedwa, magazi anga nkukhala ngati otsiridwa pa nsembe imene chikhulupiriro chanu chikupereka kwa Mulungu. Ngati ndi choncho ndili wokondwa, ndipo ndikusangalala nanu pamodzi nonsenu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:5

Inunso mukhale ngati miyala yamoyo yoti Mulungu amangire nyumba yake. M'menemo muzitumikira ngati ansembe opatulika, pakupereka nsembe zochokera ku mtima, zokomera Mulungu kudzera mwa Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:24

Atatero Yesu adauza ophunzira ake kuti, “Munthu wofuna kutsata Ine, adzikane mwiniwakeyo, ndipo asenze mtanda wake nkumanditsata.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 107:22

Apereke nsembe zothokozera, ndi kulalika ntchito za Chauta, poimba nyimbo zachimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 29:18

Ndipo upsereze nkhosa yonseyo paguwapo. Imeneyo idzakhala nsembe yopsereza yopereka kwa Chauta. Idzakhala nsembe ya fungo lokoma yopereka pa moto kwa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:20

Mwa Iyeyo Mulungu adafuna kuyanjanitsanso zinthu zonse ndi Iye mwini, zapansipano ndi za Kumwamba. Adachita zimenezi pakudzetsa mtendere kudzera mwa imfa ya Mwana wake pa mtanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:32

Iye sadaumire ngakhale Mwana wakewake, koma adampereka chifukwa cha ife tonse. Atatipatsa Mwana wakeyo, nanga Iye nkulephera kutipatsanso zonse mwaulere?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 20:3

Alandire zopereka zako zonse, akondwere ndi nsembe zako zopsereza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 4:27-31

“Ngati munthu wamba aliyense achimwa mosadziŵa, pochita china chilichonse chimene Chauta amaletsa, napalamula pakutero, tchimo lakelo akalizindikira, apereke nsembe ya mbuzi yaikazi yopanda chilema, chifukwa cha tchimo lakelo. Tsono asanjike dzanja lake pamutu pa mbuzi ya nsembe yopepesera machimoyo, ndipo aiphere pa malo amene amaperekera nsembe yopsereza. wochimwayo akakhala wansembe wodzozedwa, pakutero wausandutsa wopalamula mpingo wonse, tsono azipereka kwa Chauta ng'ombe yaing'ono yamphongo yopanda chilema, chifukwa cha tchimo lakelo. Imeneyo ndiyo nsembe yopepesera machimo ake. Atatero, wansembe atengeko magazi ndi chala chake, ndi kuŵapaka pa nyanga za guwa la nsembe zopsereza, ndipo magazi otsalawo aŵathire patsinde pa guwa lomwelo. Tsono achotse mafuta ake onse, monga momwe amachotsera mafuta a nsembe yachiyanjano, ndipo wansembe aŵatenthe pa guwalo, kuti atulutse fungo lokomera Chauta. Wansembeyo atachita mwambo wopepesera machimo a munthu wamba uja, munthuyo adzakhululukidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:15

Nchifukwa chake, kudzera mwa Yesu tiyeni tipereke kosalekeza mayamiko athu kwa Mulungu ngati nsembe. Ndiye kunena kuti tipereke ngati nsembe mau athu ovomereza dzina lake poyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:2

Iyeyo ndiye nsembe yopepesera machimo athu, ndipo osati athu okha, komanso a anthu a pa dziko lonse lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:28

Pakuti aŵa ndi magazi anga otsimikiza Chipangano cha Mulungu. Magazi ameneŵa ndiŵakhetsa chifukwa cha anthu ochuluka, kuti Mulungu aŵakhululukire machimo ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 5:21

Khristu sadachimwe konse, koma Mulungu adamsandutsa uchimo chifukwa cha ife, kuti mwa Iyeyo ife tisanduke olungama pamaso pa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:3

Kuchita zolungama ndi zokhulupirika kumakondweretsa Chauta koposa kupereka nsembe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:25

Mulungu adampereka Iyeyu kuti ndi imfa yake akhale nsembe yokhululukira machimo a anthu omkhulupirira Iye. Mulungu adachita zimenezi kuti aonetse njira yake imene anthu amapezekera kuti ngolungama pamaso pake. Zoonadi kale mwa kuleza mtima kwake sadalange kotheratu anthu ochimwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 40:6-8

Simudafune nsembe ndi zopereka, koma mwandipatsa makutu oti ndizimvera. Simudapemphe nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo. Tsono ndidati, “Ndilipo, ndikubwera, monga zidalembedwa za ine m'buku la malamulo. Ndimakonda kuchita zimene mumafuna, Inu Mulungu wanga, malamulo anu ali mumtima mwanga.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 1:11

Chauta akuti, “Kodi ndili nazo chiyani nsembe zanu zochuluka? Zandikola nsembe zopsereza za nkhosa zamphongo ndi za mafuta a nyama zonenepa. Sindikuŵafunanso magazi a ng'ombe zamphongo ndi a anaankhosa ndi a atonde.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:27

Chauta ndi Mulungu, ndipo watipatsa kuŵala. Yambani mdipiti wachikondwerero mutatenga nthambi, mpaka kukafika ku guwa lansembe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:14

Koma ine sindinganyadire kanthu kena kalikonse, koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu basi. Popeza kuti Iye adafa pa mtanda, tsopano zapansipano kwa ine zili ngati zakufa, ndipo inenso kwa zapansipano, ndili ngati wopachikidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:57

Koma tiyamike Mulungu amene amatipambanitsa mwa Ambuye athu Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:2

Muzikondana, monga Khristu adatikonda ife, nadzipereka kwa Mulungu chifukwa cha ife. Adadzipereka ngati chopereka ndi nsembe ya fungo lokondweretsa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:23-24

“Nchifukwa chake ngati wabwera ndi chopereka chako ku guwa, nthaŵi yomweyo nkukumbukira kuti mnzako wina ali nawe nkanthu, siya chopereka chakocho kuguwa komweko, ndipo pita, kayambe wayanjana naye mnzakoyo. Pambuyo pake ndiye ubwere kudzapereka chopereka chako chija.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:8

Koma Mulungu adatsimikiza kuti amatikonda kwambiri, chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu adatifera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 116:17

Ndidzapereka kwa Inu nsembe yothokozera, ndidzapemphera potchula dzina la Inu, Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:14

Mwa nsembe imodzi yomweyo wasandutsa angwiro kwamuyaya onse amene Iye akuŵayeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:10

Komabe ndi Chauta yemwe amene adaafuna kuti amuzunze, ndipo adamsautsadi. Iye adapereka moyo wake kuti ukhale nsembe yokhululukira machimo. Choncho adzaona zidzukulu zake, adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Chauta chidzachitika mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:18

Paja nayenso Khristu adafera machimo a anthu kamodzi kokha; munthu wolungama kufa m'malo mwa anthu ochimwafe, kuti atifikitse kwa Mulungu. Pa za thupi adaphedwa, koma pa za mzimu adapatsidwa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:8

Nsembe ya anthu oipa mtima imamuipira Chauta, koma pemphero la anthu olungama limamkondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 55:22

Tula kwa Chauta nkhaŵa zako, ndipo Iye adzakuchirikiza. Sadzalola konse kuti wolungama wake agwedezeke.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:29-30

Ngati diso lako la ku dzanja lamanja likuchimwitsa, likolowole nkulitaya. Ndi bwino koposa kuti utayepo chiwalo chako chimodzi, kusiyana nkuti thupi lako lonse aliponye ku Gehena. “Ngodala anthu amene ali osauka mumtima mwao, pakuti Ufumu wakumwamba ndi wao. Ndipo ngati dzanja lako lamanja likuchimwitsa, lidule nkulitaya. Ndi bwino kuti utayepo chiwalo chako chimodzi, kupambana kuti thupi lako lonse likaponyedwe ku Gehena.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 8:5

Ndipo adathandizadi mopitirira pa zimene tidaayembekeza, pakuti poyamba adadzipereka kwa Ambuye, kenaka mwa kufuna kwa Ambuye adadziperekanso kwa ife.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 50:14

“Koma perekani nsembe zanu zothokozera kwa Mulungu, ndipo muchite zimene mudalumbira kwa Wopambanazonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:4

Pokhala ndi chikhulupiriro, Abele adapereka kwa Mulungu nsembe yopambana ya Kaini, navomerezedwa kuti ngwolungama, chifukwa Mulungu mwiniwake adaamchitira umboni pakulandira zopereka zake. Mwakuti ngakhale iye adafa, koma chifukwa cha chikhulupiriro chakecho, akulankhulabe mpaka pano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 66:3

“Koma pali ena amene amangochita zoŵakomera. Kwa iwo nchimodzimodzi kupereka ng'ombe yamphongo ngati nsembe kapena kupha munthu, kupha mwanawankhosa kuti aperekere nsembe kapena kupha galu, kupereka chopereka cha chakudya kapena kupereka magazi a nkhumba, kupereka lubani ku nsembe yachikumbutso kapena kupembedza fano. Anthu ameneŵa mtima wao umakondwera nazo zonyansa zao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:1-2

Tsono abale, popeza kuti Mulungu watichitira chifundo chachikulu chotere, ndikukupemphani kuti mupereke matupi anu omwe kuti akhale nsembe yamoyo, yopatulika, ndi yokondwetsa Mulungu. Imeneyi ikhale njira yanu yopembedzera Mulungu mwauzimu. Muzikondana kwenikweni monga abale, ndipo muzichita ngati kupikisana poonetsana ulemu. Potumikira Ambuye, changu chanu chisazilale, koma chikhalebe choyaka. Muzikhala okondwa chifukwa cha chiyembekezo chanu. Muzipirira pakati pa masautso, ndipo muzipemphera nthaŵi zonse. Muzipereka zothandiza akhristu anzanu osoŵa, ndipo muziyesetsa kulandira alendo mokondwa. Pemphani Mulungu kuti aŵadalitse amene amakuzunzani. Ndithu, pemphani kuti aŵadalitse, osaŵatemberera ai. Muzikondwa nawo amene akukondwa, muzilira nawo amene akulira. Muzimvana bwino, ndipo musamadzikweze, koma muziyanjana nawo anthu wamba. Musamadziyese anzeru. Munthu akakuchitani choipa, musamubwezere choipa. Yesani kuchita zimene anthu onse amaziwona kuti nzabwino. Ngati nkotheka, khalani ndi mtendere ndi anthu onse, monga momwe mungathere. Okondedwa anga, musabwezere choipa, koma alekeni, mkwiyo wa Mulungu ndiwo uŵalange. Paja Malembo akuti, “Kulipsira nkwanga. Ndidzaŵalanga ndine, akutero Chauta.” Musamatsanzira makhalidwe a anthu odalira zapansipano, koma Mulungu asinthe moyo wanu wonse pakukupatsani mitima yatsopano. Pamenepo mudzatha kudziŵa zimene Mulungu afuna, ndipo mudzazindikira zimene zili zabwino, zangwiro ndi zomkondwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:18

Ndalandiradi zonse, ndipo ndili nazo zochuluka. Ndili ndi zonse zofunika tsopano, popeza kuti ndalandira kwa Epafrodito zimene mudanditumizira. Zili ngati chopereka cha fungo lokoma, ngati nsembe imene Mulungu ailandira ndi kukondwera nayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 9:26

Zikadatero, akadayenera kumamva zoŵaŵa kaŵirikaŵiri chilengedwere cha dziko lapansi. Koma monga zilirimu, waoneka kamodzi kokha pakutha pake pa nthaŵi yotsiriza, kuti achotse uchimo pakudzipereka yekha nsembe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 6:25-30

“Uza Aroni ndi ana ake kuti, ‘Lamulo la nsembe yopepesera machimo ndi ili: pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza, aphereponso nsembe yopepesera machimo kwa Chauta. Imeneyo ndi nsembe yoyera kopambana. Wansembe amene aiperekere machimoyo, adye nyamayo. Aidyere pa malo oyera, pa bwalo la chihema chamsonkhano. Aliyense wokhudza nsembeyo adzaonongedwa chifukwa cha mphamvu ya kuyera kwake. Tsono magazi ake akagwera pa chovala, muchape chovalacho pa malo oyera. Ndipo auphwanye mphika wadothi umene adaphikamo nyamayo. Koma akaphika wamkuŵa, autsuke mphikawo ndi kuutsukuluza ndi madzi. Munthu wamwamuna aliyense wa m'banja la ansembe angathe kudyako. Imeneyo ndiyo nsembe yoyera kopambana. kapena kunama kuti sadatole zimene zidatayika, kapena kumalumbira zonama pa kanthu kalikonse, Koma asadye nyama ya nsembe yopepesera machimo imene magazi ake amabwera nawo ku chihema chamsonkhano, kudzapepesera machimo ku malo oyera. Aitenthe pa moto imeneyo.’

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:7

Koma tikamayenda m'kuŵala, monga Iye ali m'kuŵala, pamenepo tikuyanjana tonsefe. Ndipo magazi a Yesu, Mwana wake, amatitsuka ndi kutichotsera tchimo lililonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:19

Pamenepo mudzakondwera ndi nsembe zoyenera, nsembe zootcha ndi zopsereza kwathunthu. Choncho adzapereka ng'ombe zamphongo pa guwa lanu lansembe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 22:13

Abrahamu atayang'ana, adaona kuti pali nkhosa yamphongo yogwidwa nyanga zake m'ziyangoyango. Adapita kukaigwira, naipha ngati nsembe yopsereza m'malo mwa mwana wake uja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 2:6

Iyeyo adadzipereka kuti akhale momboli wa anthu onse. Umenewu unali umboni umene udaperekedwa pa nthaŵi yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 26:6-7

Ndimasamba m'manja kuwonetsa kuti sindidachimwe, ndimakupembedzani pa guwa lanu lansembe, Inu Chauta. Ndimaimba molimbika nyimbo yothokozera, ndimalalika ntchito zanu zonse zodabwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:39

Adapita patsogolo pang'ono, nadzigwetsa choŵeramitsa nkhope pansi nkuyamba kupemphera. Adati, “Atate, ngati nkotheka, chindichokere chikho chamasautsochi. Komabe chitani zimene mukufuna Inu, osati zimene ndikufuna Ine ai.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 40:3

Mulungu waika nyimbo yatsopano m'kamwa mwanga, nyimbo yake yotamanda Iye. Anthu ambiri adzaona zimenezi ndipo adzaopa, nadzakhulupirira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:16

Musanyozere kumachita zachifundo ndi kumathandizana, chifukwa nsembe zotere zimakondweretsa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:7-9

Palibe ndi mmodzi yemwe mwa ife amene amakhala moyo chifukwa cha iye yekha, kapena kufa chifukwa cha iye yekha. Tikakhala ndi moyo, moyowo ndi wa Ambuye, tikafa, timafera Ambuye. Nchifukwa chake, ngakhale tikhale ndi moyo kapena tife, ndife ao a Ambuye. Paja Khristu adamwalira nakhalanso ndi moyo, kuti akhale Mbuye wa anthu akufa ndiponso wa anthu amoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:12

Motero Ine ndidzampatsa ulemu woyenerera akuluakulu. Adzagaŵana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza kuti adapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo adamuyesa mnzao wa anthu ophwanya malamulo. Adasenza machimo a anthu ambiri, ndipo adaŵapempherera ochimwawo kuti akhululukidwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 9:7

Aliyense apereke monga momwe adatsimikiziratu mumtima mwake, osati ndi chisoni kapena mokakamizidwa, pakuti Mulungu amakonda wopereka mokondwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:4

Pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu chuma sichithandiza konse, koma chilungamo ndiye chimapulumutsa ku imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 96:8

Tamandani ulemerero wa dzina la Chauta. Bwerani ndi zopereka, ndipo muloŵe m'mabwalo a Nyumba yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 1:4

Khristuyo adadzipereka chifukwa cha machimo athu, kuti atipulumutse ku njira za moyo woipa uno. Pakutero adachita zimene Mulungu Atate athu ankafuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:25

Chifukwa wofuna kupulumutsa moyo wake, adzautaya, koma wotaya moyo wake chifukwa cha Ine, adzaupeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 22:29-30

Pamene mupereka nsembe yothokoza Chauta, muipereke mwa njira yoti ilandiridwe. Munthu wina aliyense mwa zidzukulu zake pa mibadwo yonse, akayandikira zopatulika zimene Aisraele adazipereka kwa Chauta, pamene iyeyo ali woipitsidwa, asaonekenso pamaso panga. Ine ndine Chauta. Muidye pa tsiku lomwelo, ndipo musaisiyeko mpaka m'maŵa. Ine ndine Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:1-2

Motero tsopano palibiretu mlandu wotsutsa anthu amene amakhala mwa Khristu Yesu. Khristu akakhala mwa inu, ngakhale thupi lanu lidzafadi chifukwa cha uchimo, komabe mzimu wanu udzakhala ndi moyo, popeza kuti Mulungu wakuwonani kuti ndinu olungama pamaso pake. Ndipo Mzimu wa Mulungu, amene adaukitsa Yesu kwa akufa, akamakhala mwa inu, pamenepo, mwa Mzimu wake yemweyo, Mulungu adzapatsanso moyo matupi anu otha kufaŵa. Motero abale, tili ndi ngongole, komatu ngongole yake si yakuti tizigonjera khalidwe lathu lokonda zoipa, ndi kumachita chifuniro chake. Pakuti ngati m'moyo mwanu mutsata khalidwelo, mudzafa. Koma ngati ndi chithandizo cha Mzimu Woyera mupha zilakolako zanu zathupi, mudzakhala ndi moyo. Onse amene Mzimu wa Mulungu amaŵatsogolera, amenewo ndi ana a Mulungu. Pajatu Mzimu amene mudalandira, sakusandutsani akapolo, kuti muzikhalanso amantha ai. Koma Mzimuyo amakusandutsani ana a Mulungu, ndipo mwa mphamvu yake, popemphera kwa Mulungu timati, “Abba! Atate!” Mzimu Woyera mwiniwakeyo ndi amene amavomerezana ndi mitima yathu kutsimikiza kuti ndife ana a Mulungu. Tsono ngati ndife ana a Mulungu, tidzalandira nao madalitso amene Iye akusungira anthu ake. Pamodzi ndi Khristu ifenso tidzalandira madalitso amene Mulungu anali atamsungira. Pakuti ngati timva zoŵaŵa pamodzi ndi Khristu, tidzalandiranso ndi ulemerero womwe pamodzi naye. Ine ndikutsimikiza kuti masautso amene tikuŵamva tsopano salingana mpang'ono pomwe ndi ulemerero umene Mulungu adakonza kuti adzatiwonetse m'tsogolo muno. Zolengedwa zonse zikudikira molakalaka kuti Mulungu aonetse ana ake poyera. Pakuti lamulo la Mzimu Woyera, lotipatsa moyo mwa Khristu Yesu, landimasula ku lamulo la uchimo ndi la imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 141:2

Pemphero langa likwere kwa Inu ngati lubani, kukweza kwa manja anga kukhale ngati nsembe yamadzulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 2:17

Nchifukwa chake adaayenera kusanduka wofanafana ndi abale ake pa zonse, kuti akhale mkulu wa ansembe onse wachifundo ndi wokhulupirika potumikira Mulungu, ndipo kuti pakutero achotse machimo a anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 5:7

Muchotse chofufumitsira chakalechi cha uchimo, kuti mukhale oyera mtima ndithu, ngati buledi watsopano wosafufumitsa, monga momwe muliri ndithu, pakuti Khristu, Mwanawankhosa wathu wa Paska, adaphedwa kale ngati nsembe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:108

Chauta, landirani mapemphero anga oyamika, ndipo mundiphunzitse malangizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:2

Musamatsanzira makhalidwe a anthu odalira zapansipano, koma Mulungu asinthe moyo wanu wonse pakukupatsani mitima yatsopano. Pamenepo mudzatha kudziŵa zimene Mulungu afuna, ndipo mudzazindikira zimene zili zabwino, zangwiro ndi zomkondwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 29:42

Zopereka zopsereza zimenezi ziziperekedwa nthaŵi zonse pa mibadwo yonse. Muzizipereka pamaso pa Ine Chauta pa chipata choloŵera m'chihema chamsonkhano, kumene ndizidzakumana ndi anthu anga ndi kulankhula nawo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 27:51

Pompo chinsalu chochinga chija cha m'Nyumba ya Mulungu chidang'ambika pakatimpakati, kuyambira pamwamba mpaka pansi. Kudachita chivomezi, ndipo matanthwe adang'ambika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:13

Musapereke chiwalo chilichonse cha thupi lanu ku uchimo, kuti chigwire ntchito zotsutsana ndi chilungamo. Inu mudzipereke kwa Mulungu, monga anthu amene anali akufa, koma tsopano ali amoyo. Ndipo mupereke ziwalo zanu zonse kwa Mulungu, kuti zigwire ntchito zachilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:17

Pokhala ndi chikhulupiriro, Abrahamu, pamene Mulungu adamuyesa, adapereka Isaki ngati nsembe. Ngakhale anali munthu woti Mulungu adaampatsa lonjezo, adakhala wokonzeka kupereka ngati nsembe mwana wake mmodzi yekhayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:6

Tonse tidaasokera ngati nkhosa. Aliyense mwa ife ankangodziyendera. Ndipo Chauta adamsenzetsa iyeyo machimo athu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 4:5

Perekani nsembe zanu ndi mtima wolungama, ikani mitima yanu pa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 69:30-31

Ndidzatamanda dzina la Mulungu pomuimbira nyimbo, ndidzalalika ukulu wake pomuthokoza. Zimenezi zidzakondwetsa Chauta kupambana nsembe, ngakhale nsembe ya ng'ombe yamphongo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:24

Khristu mwiniwake adasenza machimo athu m'thupi lake pa mtanda, kuti m'machimo tikhale ngati akufa, koma pakutsata chilungamo tikhale amoyo ndithu. Mudachiritsidwa ndi mabala ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 26:9

Musanditayire kumodzi ndi anthu ochimwa, musandichotsere moyo pamodzi ndi anthu ofuna kupha anzao,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 3:18

Ndakhala ndikukuuzani kaŵirikaŵiri, ndipo tsopano ndikubwerezanso molira misozi, kuti pali ambiri amene mayendedwe ao akutsimikiza kuti amadana ndi mtanda wa Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 27:35

Atampachika pa mtanda, adagaŵana zovala zake pakuchita maere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 54:6

Ndidzapereka nsembe kwa Inu mwaufulu. Ndidzatamanda dzina lanu, Inu Chauta, popeza kuti ndinu abwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:8

Motero poyamba adati, “Nsembe kapena zopereka, nsembe zopsereza kwathunthu kapenanso nsembe zoperekera machimo, simudazifune ndipo simudakondwere nazo.” Zimenezi nzimene Malamulo adaanena kuti ziperekedwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 116:12

Ndidzambwezera chiyani Chauta pa zabwino zonse zimene adandichitira?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 29:31

Pamenepo Hezekiya adati, “Tsopano inu mwadzipereka kuti mugwire ntchito ya Chauta. Idzani pafupi, mubwere nazo nsembe ndi zopereka zothokozera ku Nyumba ya Chauta.” Msonkhanowo udabwera nazo nsembe ndi zopereka zothokozera. Anthu onse amene anali ndi mtima waufulu adabwera ndi nsembe zopsereza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:26

Koma tsopano wapereka Yesu pofuna kutsimikiza chilungamo chake, kuti anthu adziŵe kuti Iye mwini ngwolungama, adziŵenso kuti aliyense wokhulupirira Yesu amapezeka kuti ngwolungama pamaso pa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 9:14

Nanji tsono magazi a Khristu, angathe kuchita zoposa. Mwa Mzimu wamuyaya Iye adadzipereka ngati nsembe yopanda chilema kwa Mulungu. Ndiye kuti magazi ake adzayeretsa mitima yathu pakuichotsera ntchito zosapindulitsa moyo, kuti tizitumikira Mulungu wamoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 50:5

Iye akuti, “Sonkhanitsani pamaso panga, anthu anga okhulupirika, amene adachita chipangano ndi Ine popereka nsembe.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 31:54

Tsono Yakobe adapereka nsembe paphiripo, naitana anthu ake kuti adzadye chakudya. Atamaliza kudyako, adagona paphiri pomwepo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:16

pakundipatula kuti ndikhale mtumiki wa Khristu Yesu kwa anthu a mitundu ina. Adandipatsa ntchito yolalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu ngati wansembe, kuti anthuwo akhale ngati nsembe yokomera Iye ndi yoperekedwa mwa Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 130:7

Iwe Israele, khulupirira Chauta. Paja Chauta ndi wa chikondi chosasinthika, ndi wokonzeka kupulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:24

Paja mukudziŵa kuti Ambuye adzakupatsani mphotho. Mphothoyo ndi madalitso amene adalonjeza kudzapatsa anthu ake. Ambuye amene mukuŵatumikirawo ndi Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:13-15

Ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza, ndidzachitadi zimene ndidazilumbira kwa Inu, zimene ndidalankhula ndi pakamwa panga, ndiponso zimene ndidalonjeza pamene ndinali pa mavuto. Ndidzapereka kwa Inu nsembe zopsereza za nyama zonenepa, utsi wa nsembe za nkhosa zamphongo udzafika kwa Inu. Ndidzaperekanso ngati nsembe ng'ombe zamphongo ndi mbuzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 12:7

Mukadadziŵa tanthauzo la mau a Mulungu aja akuti, ‘Ndimafuna chifundo, osati nsembe ai,’ sibwenzi mutaweruza kuti ndi olakwa anthu amene sadalakwe konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 22:2

Mulungu adati, “Tenga Isaki, mwana wako mmodzi yekha uja amene umamkonda kwambiri, upite ku dziko la Moriya. Kumeneko ukampereke ngati nsembe yopsereza pa phiri limene ndidzakuuza.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 8:20

Pamenepo Nowa adamanga guwa kumangira Chauta. Adatengako mtundu uliwonse wa nyama ndi mbalame zimene anthu amaperekera nsembe, ndipo adazipha, napereka nsembe zopsereza paguwapo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:12

Koma Khristu adapereka nsembe imodzi yokha yochotsera machimo onse. Ndipo ataipereka, adakakhala ku dzanja lamanja la Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 17:11

Pakuti moyo wake wa cholengedwa chilichonse uli m'magazi, ndipo ndaŵapereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amene amachotsa machimo, chifukwa cha moyo umene umakhala m'magazimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 4:35

Tsono achotse mafuta ake onse, monga momwe amachotsera mafuta a nkhosa yoperekera nsembe yachiyanjano. Ndipo aŵatenthe pa guwa, pamodzi ndi nsembe zina zopsereza pa moto, zopereka kwa Chauta. Umu ndimo m'mene wansembe azichitira mwambo wopepesera tchimo la munthu, ndipo munthuyo adzakhululukidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 5:10

Ndipo apereke mbalame inayo kuti ikhale nsembe yopsereza, potsata mwambo wake. Wansembe atachita mwambo wopepesera machimo amene munthuyo wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 3:21

Ndipo Chauta adasokera Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa naŵaveka onse aŵiriwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 4:4

Abele nayenso adatenga ana oyamba kubadwa a nkhosa zake, naŵapereka ngati nsembe, pamodzi ndi mafuta ake omwe. Tsono Chauta adakondwera ndi Abele, nalandira nsembe yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 16:30

Pajatu pa tsiku limenelo padzakhala mwambo wopepesera machimo anu, kuti machimo anu achotsedwe. Choncho mudzakhala oyera pamaso pa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 16:15

“Tsono Aroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu. Magazi ake aloŵe nawo kuseri kwa nsalu yochinga, ndi kuchita nawo monga momwe adachitira ndi magazi a ng'ombe, pakuwaza magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 12:13

Magaziwo adzakhala chizindikiro pa nyumba zimene mumakhalamo. Ndikadzangoona magaziwo, ndidzakupitirirani inuyo, ndipo mliri wosakaza sudzakugwerani, pamene ndidzakanthe dziko la Ejipito.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu wanga, ndimakukondani ndipo ndikuthokozani chifukwa cha chikondi chanu chopanda malire ndi chifundo chanu. Zikomo chifukwa cha kukoma mtima kwanu kwa ine, nthawi zonse mumandionetsera chifundo chanu. Ambuye Yesu, zikomo chifukwa chobwera kudziko lino kudzandipulumutsa ku uchimo ndi kundipatsa moyo wosatha. Ambuye, zikomo chifukwa cha nsembe iliyonse yomwe mudapereka kuti ine ndikhale womasuka ku imfa. Mzimu Woyera, mundiphunzitse kupereka nsembe yoyamika tsiku lililonse, mosasamala kanthu za mavuto omwe ndikukumana nawo. Monga Paulo ndi Sila, ndikhale ndi nyimbo mkamwa mwanga kuti zitseko zitseguke. Ndifuna kupereka nsembe yachikondi kwa inu monga Abrahamu. Ndisungeni ndikukulemekezani Mulungu, monga momwe Davide anachitira. Atate, m'dzina la Yesu, ndikupemphani kuti munditsogolere ndi kuyika chikondi ndi chidziwitso mumtima mwanga kuti ndipereke nsembe zoyenera kwa inu monga momwe Abele anachitira. Munditsuke ndi kundiyera ndi magazi anu Yesu kuti ndikhale woyenera pamaso pa Mulungu wanga ndi kukusondweretsani nthawi zonse. Inu wokondedwa wanga ndinu chitsanzo chachikulu cha nsembe, pakuti lemba limati: "koma Khristu atapereka nsembe imodzi yokha ya machimo nthawi zonse, anakhala pansi kudzanja lamanja la Mulungu." Zikomo Ambuye chifukwa cha chikhulupiriro chomwe mwandipatsa, zikomo chifukwa choti ndinu chitsanzo changa cha chikondi, cha chikhululukiro, ndi cha nsembe. Zikomo Ambuye chifukwa cha moyo wanga, banja langa, nyumba yanga, anzanga, chifukwa chondiletsa kugawana zonse zomwe mumandipatsa nawo. Zikomo Ambuye chifukwa cha kukoma mtima kwanu kopanda malire ndi chikhululukiro, m'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa