Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

103 Mau a Mulungu Okhudza Chilengedwe

Poyamba, Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi (Genesis 1:1). Mawu akuti “analenga” amandipangitsa kuganizira mphamvu zazikulu za Mulungu zolenga, chifukwa amandiuza kuti Iye analenga chilengedwe chonse. Kulenga ndi mphamvu ya Mulungu yekha. Palibe wina amene angalenge; sitinachokere ku kusanduka kwa zinthu, koma ndife ntchito ya manja a Mulungu Wamphamvuyonse.

Chifukwa ndife ntchito yake, lolengedwa mwa Khristu Yesu kuti tichite ntchito zabwino, zimene Mulungu anakonzeratu kale kuti tiyendemo (Aefeso 2:10). Mphamvu yaikulu ya Mulungu ikuwonekera m’chilengedwe chake, ndipo timaiwonanso m’magonjetso ake onse pa mdima, koma chikondi chake ndiye chachikulu kuposa zonse. Chifukwa cha chikondi anatumiza Mwana wake, ndipo chifukwa cha chikondi Yesu anapereka moyo wake pa mtanda chifukwa cha machimo athu.

Uyenera kumvetsa kuti unalengedwa kuti uchite zabwino. Cholinga cha Mulungu ndi chakuti uziyenda padziko lapansi monga momwe Yesu anachitira. Iye nthawi zonse ankachita zabwino ndi kuyenda molungama m’njira za Atate wake. Chilengedwe chokha chikuwonetsa ukulu wa Mulungu; chilengedwe chimanena za Iye. Ndipo ife, amene tapatsidwa ntchito yogwirizanitsa dziko lino ndi Khristu, tiyenera kuchita zambiri.

Uyenera kumvetsa kuti sunalengedwa kungobadwa, kukula ndi kufa. Sunalengedwa kuti ukhale tsiku ndi tsiku osaganizira momwe ukugwiritsira ntchito nthawi yako. Unalengedwa ndi dzanja la Mulungu, uli ndi moyo chifukwa cha mpweya wa Mzimu wake kuti ukhudze anthu ena m’moyo wako watsiku ndi tsiku. Ndinu mwamuna ndi mkazi oitanidwa kuwonetsa mphamvu ya Mulungu yolenga. Uyenera kukhala chifaniziro chake padziko lapansi ndi kulamulira zinthu zonse.

Ukadziwa kuti ulipo chifukwa cha Mulungu, umadziwa kuti uli ndi mwini wake ndipo uyenera kukhala nthawi zonse kuti uchite chifuniro chake. Akolose 1:16 amati: “Pakuti mwa Iye zinthu zonse zinalengedwa, zakumwamba ndi zapadziko lapansi, zowoneka ndi zosaoneka; kaya mipando yaufumu, kaya maufumu, kaya maulamuliro, kaya maboma; zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye, ndipo zinalengedwera Iye.”

Sunalengedwa kuti udzisangalatse ndi zokondweretsa zako ndi kuchita zoipa, koma unalengedwera Mulungu, ndi Iye, kuti uchite zinthu zazikulu padziko lapansi.


Masalimo 19:1

Zakumwamba zimalalika ulemerero wa Mulungu, thambo limasonyeza ntchito za manja ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:28

Kodi sudziŵa? Kodi sudamve? Chauta ndiye Mulungu wachikhalire, Mlengi wa dziko lonse lapansi. Satopa kapena kufooka, palibe amene amadziŵa maganizo ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:26-27

Zitatha izo Mulungu adati, “Tiyeni tipange munthu m'chifanizo chathu, adzakhale wonga Ifeyo. Adzalamulire nsomba zam'nyanja, mbalame zamumlengalenga, nyama zoŵeta, ndi zokwaŵa zonse za pa dziko lapansi.”

Motero Mulungu adalenga munthu, m'chifanizo chake, adaŵalengadi m'chifanizo cha Mulungu. Adaŵalenga wina wamwamuna wina wamkazi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 38:4

“Kodi udaali kuti pamene ndinkaika maziko a dziko lapansi? Undiwuze ngati ndiwe womvetsa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 45:12

Ndine amene ndidalenga dziko lapansi ndi kulenga munthu kuti akhalemo. Ndidayalika zakuthambo ndi manja anga, ndipo tsopano ndimalamulira gulu lonse lamumlengalenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 2:1-2

Motero dziko lonse lapansi, thambo ndi zonse zokhala m'menemo, zidatha kulengedwa.

Mtsinje wotuluka mu Edeni momwemo, unkayenda numathirira mundawo. Mtsinjewo udagaŵika panai, nusanduka mitsinje inai.

Mtsinje woyamba ndi Pisoni, ndipo umayenda mozungulira dziko la Havila, kumene kumapezeka golide.

(Golide wakumeneko ndi wabwino. Kumapezekanso bedeliyo ndi miyala ya mtengowapatali yotchedwa onikisi.)

Mtsinje wachiŵiri ndi Gihoni, ndipo umayenda mozungulira dziko la Kusi.

Mtsinje wachitatu ndi Tigrisi, umene umayenda kuvuma kwa Asiriya. Mtsinje wachinai ndi Yufurate.

Tsono Chauta adamtenga munthuyo, namukhazika m'munda wa Edeni uja kuti azilima ndi kumausamala.

Ndipo Chauta adamlamula munthuyo kuti, “Uzidya zipatso za mtengo uliwonse wam'mundawu,

kupatula mtengo wokhawo umene umadziŵitsa zabwino ndi zoipa. Zipatso za mtengo umenewo usadye. Ukadzadya, ndithu udzafa!”

Pambuyo pake Chauta adati, “Sibwino kuti munthuyu akhale yekha. Ndipanga mnzake woti azimthandiza.”

Chauta adatenga dothi naumba nyama zonse ndi mbalame zonse, nabwera nazo kwa Adamu kuti azitche maina. Mwakuti maina amene Adamu adazitcha, maina ake ndi omwewo.

Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi Mulungu adamaliza ntchito imene ankachitayo, ndipo adapumula pa tsiku lachisanu ndi chiŵiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 104:24-25

Inu Chauta ntchito zanu nzambiri, zonse mwazipanga mwanzeru, ndipo dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.

Kuli nyanja yaikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zinthu zosaŵerengeka, zinthu zamoyo, zazing'ono ndi zazikulu zomwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 19:4

Yesu adaŵayankha kuti, “Kodi simunaŵerenge kuti Mulungu amene adalenga anthu pa chiyambi, adalenga wina wamwamuna, wina wamkazi?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 148:1-5

Tamandani Chauta! Tamandani Chauta inu okhala kumwamba, mtamandeni inu okhala mu mlengalenga!

Inu nyama zakutchire ndi zoŵeta zonse, inu zinthu zokwaŵa ndi mbalame zouluka!

Inu mafumu a pa dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse, inu akuluakulu ndi olamulira dziko lapansi!

Inu anyamata pamodzi ndi anamwali, inu nkhalamba ndi ana omwe!

Onsewo atamande dzina la Chauta, pakuti dzina lake lokha nlolemekezeka, ulemerero wake ndi woposa, pansi pano nkumwamba komwe.

Chauta wakweza anthu ake poŵapatsa mphamvu. Walemekeza anthu ake onse oyera mtima, Aisraele amene Iye amaŵakonda. Tamandani Chauta!

Mtamandeni inu angelo ake onse, mtamandeni inu magulu a ankhondo ake onse!

Mtamandeni inu dzuŵa ndi mwezi, mtamandeni inu nonse nyenyezi zoŵala!

Mtamandeni inu thambo lakumwambamwamba, ndi inu madzi a pamwamba pa thambo!

Zonsezo zitamande dzina la Chauta! Paja Iye adaalamula, izo nkulengedwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:3

Tsono Mulungu adati, “Kuyere,” ndipo kudayeradi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 8:3-4

Ndikamayang'ana ku thambo lanu limene mudapanga ndi manja anu, ndikamaona mwezi ndi nyenyezi zimene mudazikhazika kumeneko,

ndimadzifunsa kuti, “Kodi munthu nchiyani kuti muzimkumbukira, mwana wa munthu nchiyani kuti muzimsamalira?”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 42:5

Mulungu, Chauta, adalenga zakuthambo ndi kuziyalika. Adalenga dziko lapansi ndi zonse zimene limabereka. Adapatsa mpweya kwa anthu okhala m'dzikomo, ndi kuninkha moyo kwa onse oyendamo. Iyeyo akunena kuti,

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 26:7

Mulungu adayala thambo lakumpoto pa phompho, adakoloŵeka dziko lapansi m'malo mwake, pamene panali popanda nkanthu komwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:14

Ndikukutamandani, Inu oopsa ndi odabwitsa. Ntchito zanu zonse nzodabwitsa. Mumandidziŵa bwino kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:14-19

Pambuyo pake Mulungu adati, “Kuthambo kukhale miyuni kuti izilekanitsa usana ndi usiku, ndiponso kuti ikhale zizindikiro za nyengo, masiku ndi zaka.

Miyuni imeneyi ikhale ku thambo ndi kumaunikira dziko lapansi,” ndipo zidachitikadi.

Motero Mulungu adalenga miyuni iŵiri yaikulu: dzuŵa loŵala masana, ndi mwezi woŵala usiku. Adalenganso nyenyezi.

Mulungu adaika miyuniyo ku thambo, kuti iziwunikira dziko lapansi,

kuti iziŵala usana ndi usiku, kulekanitsa kuyera ndi mdima. Mulungu adaona kuti zinali zabwino.

Ndipo kudali madzulo ndiponso m'maŵa, tsiku lachinai.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:19

Pamene adakhazikitsa dziko lapansi, Chauta adaonetsa nzeru. Pamene adakhazikitsa zakumwamba, adaonetsa nzeru za kumvetsa bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:5

Nyanja ndi yake, popeza kuti ndiye adailenga. Mtunda ndi wakenso, popeza kuti ndiye adaupanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:21-22

Monga simudadziŵe? Monga simudamve? Kodi poyamba ponse sadakuuzeni? Kodi simudamvetse za kakhazikitsidwe ka dziko lapansi?

Dziko lapansi lidalengedwa ndi Iye amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba, kuseri kwa mlengalenga. Amaona anthu pansi ngati ziwala. Adafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchingira, ngati hema lokhalamo anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:20-22

Zitatero Mulungu adati, “M'nyanja mukhale zamoyo zambirimbiri, ndipo pakhale mbalame zouluka mu mlengalenga.”

Motero Mulungu adalenga nsomba zazikulu zam'nyanja, pamodzi ndi zolengedwa zina zonse zokhala m'madzi, ndiponso mbalame ndi zouluka zina zamitundumitundu. Mulungu adaona kuti zonse zimene adalengazo zinali zabwino.

Adazidalitsa ponena kuti, “Swanani ndipo mudzaze nyanja, mbalamenso ziswane pa dziko.”

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 3:11

Adapanga chinthu chilichonse kuti chikhale chabwino pa nthaŵi yake. M'mitima mwa anthu Mulungu adaikanso nzeru zotanthauzira zochitika za pa mibadwo ndi mibadwo. Komabe anthuwo sangathe kuzitulukira ntchito zonse za Mulungu kuyambira pa chiyambi mpaka pomalizira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 104:5

Mudakhazika dziko lapansi pa maziko ake, kuti lisagwedezeke konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 4:17

Paja Malembo akuti, “Ndakuika kuti ukhale kholo la mitundu yambiri ya anthu.” Lonjezo limeneli Abrahamu adalilandira kwa Mulungu mwini amene iye ankamukhulupirira. Ndi Mulungu amene amabwezera moyo kwa akufa, ndipo amapereka moyo kwa zinthu zopanda moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 136:5-9

Adalenga zakumwamba ndi nzeru zake, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Adayala dziko lapansi pa madzi, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Adalenga miyuni yaikulu yamumlengalenga, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Dzuŵa kuti lizilamulira usana, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Mwezi ndi nyenyezi kuti zizilamulira usiku, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:24-25

Ndipo Mulungu adati, “Padziko pakhale mitundu yonse ya zamoyo potsata mitundu yake: zoŵeta, zokwaŵa, ndi nyama zakuthengo, potsata mitundu yake.” Ndipo zidachitikadi.

Pomwepo Mulungu adalenga nyama zakuthengo potsata mitundu yake, ndi nyama zoŵeta potsata mitundu yake, ndiponso zokwaŵa zonse potsata mitundu yake. Mulungu adaona kuti zonse zimene adalengazo zinali zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:4-5

Amadziŵa chiŵerengero cha nyenyezi, zonse amazitcha maina ake.

Mbuye wathu ndi wamkulu, ndipo ndi wa mphamvu zambiri, nzeru zake nzopanda malire.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 66:1

Chauta akunena kuti, “Thambo lam'mwamba ndiye mpando wanga waufumu, dziko lapansi ndiye chopondapo mapazi anga. Kodi ndi nyumba yotani imene mungathe kundimangira inu? Ndi malo otani amene inu mungandikonzere kuti Ine ndizipumulirapo?

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:17

Iyeyo analipo zinthu zonse pakadalibe, mwa Iye zinthu zonse zimalunzana pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 148:6

Adazikhazikitsa kuti zikhale mpaka muyaya, adaikapo lamulo limene silingathe kusinthika.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:12

Motero panthaka padamera zomera za mitundu yonse, zipatso zokhala ndi njere ndi mitengo yobeleka zipatso za njere, malingana ndi mitundu yao. Mulungu adaona kuti zinali zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 104:19

Inu mudapanga mwezi kuti uzisiyanitsa nyengo, ndipo dzuŵa limadziŵa nthaŵi yake yoloŵera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 45:18

Akutero Chauta amene adalenga zakumwamba, ndi Iyeyo Mulungu amene adaumba ndi kulenga dziko lapansi, ndipo adalikhazikitsa mwamphamvu. Sadalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma kuti likhale malo okhalamo anthu. Iyeyo akunena kuti: “Chauta ndine, palibenso wina ai.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:22

Tamandani Chauta, inu zolengedwa zake zonse, ku madera onse a ufumu wake. Nawenso mtima wanga, tamanda Chauta!

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:26

Onani mbalame zamumlengalenga. Sizifesa kapena kukolola kapena kututira m'nkhokwe ai. Komabe Atate anu akumwamba amazidyetsa. Nanga inu sindinu amtengowapatali kuposa mbalame?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 104:31

Ulemerero wa Chauta ukhalebe mpaka muyaya, Chauta akondwe nazo ntchito zakezo,

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 37:14-16

“Inu aYobe, tamvani izi, imani, muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.

Kodi mukudziŵa m'mene Mulungu amazichitira, ndi m'mene amang'anipitsira mphezi m'mitambo yake?

Kaya mukudziŵa m'mene Mulungu amayalira mitambo, ntchito yosonyeza nzeru zake zodabwitsa,

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:28

Adaŵadalitsa poŵauza kuti, “Mubereke ndi kuchulukana, mudzaze dziko lonse lapansi ndi kumalilamulira. Ndakupatsani ulamuliro pa nsomba, mbalame ndi nyama zonse zimene zikukhala pa dziko lapansi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 121:2

Chithandizo changa nchochokera kwa Chauta, amene adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:22-23

“Chauta adandilenga ine nzeru pa chiyambi cha ntchito zake. Mwa ntchito zake zakalekale woyambirira ndinali ine.

Ndidapangidwa masiku akalekale, pachiyambiyambi, dziko lapansi lisanalengedwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:29-30

Ndipo Mulungu adati, “Ndikukupatsani zomera zonse za mtundu wokhala njere, ndi mitundu yonse ya zomera zobala zipatso zanjere, kuti muzidya.

Tsono Mulungu adati, “Kuyere,” ndipo kudayeradi.

Koma nyama zonse zakuthengo, mbalame, ndi zokwaŵa zonse, ndazipatsa msipu kuti zizidya,” ndipo zidachitikadi momwemo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 148:3

Mtamandeni inu dzuŵa ndi mwezi, mtamandeni inu nonse nyenyezi zoŵala!

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 38:8

Akuti, ‘Chithunzithunzi chimene dzuŵa likuchititsa pa makwerero a Ahazi, ndidzachibweza m'mbuyo makwerero khumi.’ ” Ndipo chithunzithunzicho chidabwereradi m'mbuyo makwerero khumi.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:4

Mulungu adaona kuti kuyerako kunali kwabwino. Pomwepo adalekanitsa kuyerako ndi mdima.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:15-16

Mapangidwe anga sadabisike pamaso panu pamene ndinkapangidwa mwachinsinsi, pamene ndinkaumbidwa mwaluso m'mimba mwa amai anga.

Maso anu adandiwona ndisanabadwe. Masiku a moyo wanga mudaŵalemberatu m'buku mwanu, asanayambe nkuŵerengedwa komwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:26

Yang'anani kumlengalenga. Kodi ndani adalenga nyenyezi mukuziwonazi? Ndiye amene amazitsogolera ngati gulu lankhondo, ndipo iliyonse amaiitana ndi dzina lake. Popeza kuti nyonga ndi mphamvu zake nzazikulu. Palibe ndi imodzi yomwe imene imasoŵapo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 104:14-15

Mumameretsa udzu kuti ng'ombe zidye, ndi zomera kuti munthu azilima ndi kupeza chakudya m'nthaka.

Amapezamo vinyo wosangalatsa mtima wake, mafuta odzola kuti thupi lake lisisire, ndiponso buledi kuti ampatse mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:5

Kuyerako adakutcha Usana, mdima uja adautcha Usiku. Ndipo kudali madzulo ndiponso m'maŵa, tsiku loyamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 11:5

M'mene mzimu umaloŵera m'thupi la mwana m'mimba mwa mkazi wodwala, inu simudziŵa. Chonchonso ntchito ya Mulungu amene amapanga zonse, inu simungaidziŵe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 24:1-2

Dziko lapansi ndi zonse zam'menemo ndi za Chauta, dziko lonse lapansi pamodzi ndi anthu onse okhalamo ndi ake.

Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Ndi Chauta Wamphamvuzonse. Iyeyo ndiye Mfumu yaulemerero.

Pakuti iye ndi amene adaika dziko lapansi pa nyanja yaikulu, adalikhazika pa mitsinje yozama.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 44:24

Chauta, Mpulumutsi wako, amene adakupanga m'mimba mwa mai wako, akunena kuti, “Ndine Chauta, amene ndidapanga zinthu zonse. Pamene ndinkayalika zakuthambo, ndinali ndekha. Pamene ndinkalenga dziko lapansi, kodi analipo amene adandithandiza?

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:10

Mulungu adautcha mtundawo Dziko, madzi adaŵasonkhanitsa aja adaŵatcha Nyanja. Mulungu adaona kuti zinali zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 148:1-2

Tamandani Chauta! Tamandani Chauta inu okhala kumwamba, mtamandeni inu okhala mu mlengalenga!

Inu nyama zakutchire ndi zoŵeta zonse, inu zinthu zokwaŵa ndi mbalame zouluka!

Inu mafumu a pa dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse, inu akuluakulu ndi olamulira dziko lapansi!

Inu anyamata pamodzi ndi anamwali, inu nkhalamba ndi ana omwe!

Onsewo atamande dzina la Chauta, pakuti dzina lake lokha nlolemekezeka, ulemerero wake ndi woposa, pansi pano nkumwamba komwe.

Chauta wakweza anthu ake poŵapatsa mphamvu. Walemekeza anthu ake onse oyera mtima, Aisraele amene Iye amaŵakonda. Tamandani Chauta!

Mtamandeni inu angelo ake onse, mtamandeni inu magulu a ankhondo ake onse!

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 26:6

Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu, ndipo kumeneko sikuphimbika kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 102:25

Inu mudaika maziko a dziko lapansi kalekale, ndipo zakumwamba mudazipanga ndi manja anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:19-20

Mulungu amaŵakwiyira, chifukwa zimene munthu angathe kudziŵa zokhudza Mulungu iwo akuzidziŵa bwino lomwe, popeza kuti Mulungu mwini ndiye adaŵaululira zimenezi.

Uthengawu Iye adaulonjeza kale kudzera mwa aneneri ake ndipo udalembedwa m'Malembo Oyera.

Pajatu chilengedwere cha dziko lapansi anthu akhala akuzindikira makhalidwe osaoneka a Mulungu, ndiye kuti mphamvu zake zosatha, ndiponso umulungu wake. Akhala akuzizindikira poona zimene Mulungu adalenga. Choncho alibe konse pozembera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 38:31-33

“Kodi Nsangwe iwe ungazimange maunyolo? Kodi zingwe za Akamwiniatsatana iwe ungathe kuzimasula?

Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake? Kodi ungathe kutsogolera nyenyezi yaikulu ya Chimbalangondo pamodzi ndi tiana take?

Kodi malamulo a mlengalenga umaŵadziŵa? Nanga ulamuliro wake, kodi ungaukhazikitse pa dziko lapansi?

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:15

Mitundu ya anthu ili ngati kadontho ka madzi mu mtsuko, ilinso ngati fumbi chabe pa sikelo. M'manja mwa Chauta zilumba nzopepuka ngati fumbi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 104:1-4

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga. Inu Chauta, Mulungu wanga, ndinu aakulu kwambiri. Mumavala ulemu ndi ufumu.

Inu mumatumphutsa akasupe m'zigwa, mitsinje imayenda pakati pa mapiri.

Imapatsa nyama zonse zakuthengo madzi akumwa, mbidzi zimapherapo ludzu.

Mbalame zimamanga zisa pafupi ndi mitsinjeyo, zimaimba m'nthambi za mitengo.

Inu mumathirira mapiri ndi madzi ochokera ku malo anu akumwamba. Dziko lapansi ladzaza ndi madalitso anu.

Mumameretsa udzu kuti ng'ombe zidye, ndi zomera kuti munthu azilima ndi kupeza chakudya m'nthaka.

Amapezamo vinyo wosangalatsa mtima wake, mafuta odzola kuti thupi lake lisisire, ndiponso buledi kuti ampatse mphamvu.

Mitengo ya Chauta amaithirira ndi madzi ambiri, mikungudza ya ku Lebanoni imene adaibzala.

Mbalame zimamanga zisa m'menemo, dokowe amamanga chisa m'mikungudzamo.

M'mapiri aatali ndimo m'mene mumakhala mbalale, m'matanthwe ndimo m'mene mumathaŵira mbira.

Inu mudapanga mwezi kuti uzisiyanitsa nyengo, ndipo dzuŵa limadziŵa nthaŵi yake yoloŵera.

Mumadzifunditsa ndi kuŵala ngati chovala, mwatambasula mlengalenga ngati hema.

Mumapanga mdima nukhala usiku, ndipo nyama zam'nkhalango zimatuluka.

Misona ya mikango imabangula pofunafuna nyama, kupempha chakudya kwa Mulungu.

Dzuŵa likamatuluka, imabwerera nkukagona m'mapanga mwake.

Munthu amapita ku ntchito yake, amakagwira ntchito mpaka madzulo.

Inu Chauta ntchito zanu nzambiri, zonse mwazipanga mwanzeru, ndipo dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.

Kuli nyanja yaikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zinthu zosaŵerengeka, zinthu zamoyo, zazing'ono ndi zazikulu zomwe.

Zombo zimayendamo pamodzi ndi Leviyatani, chilombo chija chimene mudachilenga kuti chiziseŵera m'madzimo.

Zonse zolengedwa zimayang'anira kwa Inu, kuti muzipatse chakudya pa nyengo yake.

Mukazipatsa zimachilandira; mukafumbatula dzanja lanu, zimakhuta.

Mukazibisira nkhope yanu, zimachita mantha ndi kutaya mtima. Mukazichotsera mpweya, zimafa nkubwerera ku fumbi.

Mwamanga Nyumba yanu pa madzi akumwamba, mitambo yaliŵiro ili ngati galeta lanu, mumayenda pa mapiko a mphepo,

Mukatumiza mpweya wanu zimalengedwa, ndipo mumakonzanso maonekedwe a dziko lapansi.

Ulemerero wa Chauta ukhalebe mpaka muyaya, Chauta akondwe nazo ntchito zakezo,

Iye amati akayang'ana dziko lapansi, limanjenjemera, akakhudza mapiri, mapiriwo amafuka nthunzi.

Ndidzaimbira Chauta moyo wanga wonse. Ndidzaimba nyimbo zotamanda Chauta, nthaŵi zonse pamene ndili moyo.

Mapemphero anga amkomere Chauta, popeza kuti ndimakondwa mwa Iye.

Anthu ochimwa aonongeke pa dziko lapansi, anthu oipa asakhaleponso. Tamanda Chauta, iwe mtima wanga. Tamanda Chauta.

Mphepo mumazisandutsa amithenga anu, malaŵi amoto mumaŵasandutsa atumiki anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 2:4

Ndimo m'mene dziko lapansi ndi zonse zakuthambo zidalengedwera. Pamene Chauta ankalenga dziko lapansi ndi zonse zakuthambo,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 104:25-26

Kuli nyanja yaikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zinthu zosaŵerengeka, zinthu zamoyo, zazing'ono ndi zazikulu zomwe.

Zombo zimayendamo pamodzi ndi Leviyatani, chilombo chija chimene mudachilenga kuti chiziseŵera m'madzimo.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:29-31

Suja amagulitsa atimba aŵiri kandalama kamodzi? Komabe palibe ndi m'modzi yemwe amene angagwe pansi, Atate anu osadziŵa.

Filipo ndi Bartolomeo; Tomasi ndi Mateyo, wokhometsa msonkho uja; Yakobe, mwana wa Alifeyo, ndi Tadeyo;

Inuyotu ngakhale tsitsi lomwe la kumutu kwanu adaliŵerenga lonse.

Choncho musati muziwopa ai. Ndinu a mtengo woposa atimba ambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:10-12

Zamoyo zonse zidzakuthokozani, Inu Chauta, anthu anu onse oyera mtima adzakutamandani.

Adzalankhula za ulemerero wa ufumu wanu, adzasimba za mphamvu zanu,

kuti adziŵitse anthu onse za ntchito zanu zamphamvu, kutinso asimbe za ulemerero ndi za ufumu wanu waukulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 26:13

Ndi mpweya mwake adayeretsa zamumlengalenga, ndi dzanja lake adapha chinjoka chothaŵa chija.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:4-5

Maziko ozama a dziko lapansi ali m'manja mwake. Mapiri aatali omwe ngakenso.

Nyanja ndi yake, popeza kuti ndiye adailenga. Mtunda ndi wakenso, popeza kuti ndiye adaupanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:7

Motero Mulungu adalenga cholekanitsa madzi chija, naŵagaŵa madziwo, ena pansi pa cholekanitsacho ena pamwamba pake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:19-22

Zolengedwa zonse zikudikira molakalaka kuti Mulungu aonetse ana ake poyera.

Pakuti lamulo la Mzimu Woyera, lotipatsa moyo mwa Khristu Yesu, landimasula ku lamulo la uchimo ndi la imfa.

Pakuti zolengedwazo zidaasanduka zogonjera zopanda pake, osati chifukwa zidaafuna kutero ai, koma chifukwa Mulungu adaagamula choncho. Komabe zili ndi chiyembekezo ichi,

chakuti izonso zidzamasulidwa ku ukapolo wa kuwola, ndi kulandirako ufulu ndi ulemerero wa ana a Mulungu.

Tikudziŵa kuti mpaka tsopano zolengedwa zonse zakhala zikubuula ndi kumva zoŵaŵa, zonga za mkazi pa nthaŵi yake yochira.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:15

Miyuni imeneyi ikhale ku thambo ndi kumaunikira dziko lapansi,” ndipo zidachitikadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 148:4

Mtamandeni inu thambo lakumwambamwamba, ndi inu madzi a pamwamba pa thambo!

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:27

Ine ndinalipo kale, pamene ankakhazikitsa zakumwamba, pamene ankalemba mzere wa malire a nyanja yozama,

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 38:9

Ndinetu amene ndidakuta nyanjayo ndi mitambo, ndidaiveka mdima ngati chovala.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 104:16

Mitengo ya Chauta amaithirira ndi madzi ambiri, mikungudza ya ku Lebanoni imene adaibzala.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 66:22

“Monga momwe dziko lapansi latsopano ndi dziko lakumwamba latsopano, zimene ndidzapange, zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, chonchonso zidzukulu zanu ndi dzina lanu zidzakhala mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 136:5

Adalenga zakumwamba ndi nzeru zake, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:18

kuti iziŵala usana ndi usiku, kulekanitsa kuyera ndi mdima. Mulungu adaona kuti zinali zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:9

pakuti Iye adalankhula, ndipo zidachitikadi, adalamula, ndipo zidaonekadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:29-31

Amalimbitsa ofooka, ndipo otopa amaŵaonjezera mphamvu.

Kukumveka mau akuti, “Konzani njira ya Chauta m'thengo, lungamitsani mseu wa Mulungu wathu m'chipululu.

Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufooka, ngakhale anyamata amaphunthwa ndi kugwa.

Koma amene amakhulupirira Chauta adzalandira mphamvu zatsopano, adzauluka ngati ziwombankhanga. Adzathamanga koma osatopa, adzayenda koma osalefuka konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 102:26

Zonsezi zidzatha ngati malaya, koma Inu mulipobe. Inu mumazisintha ngati chovala, ndipo zimatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:13

Ndipo kudali madzulo ndiponso m'maŵa, tsiku lachitatu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:19

Chauta wakhazikitsa mpando wake wachifumu kumwamba, ndipo amalamulira zonse mu ufumu wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:16

Mumafumbatula dzanja lanu, ndipo mumapatsa chamoyo chilichonse zofuna zake.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:21

Motero Mulungu adalenga nsomba zazikulu zam'nyanja, pamodzi ndi zolengedwa zina zonse zokhala m'madzi, ndiponso mbalame ndi zouluka zina zamitundumitundu. Mulungu adaona kuti zonse zimene adalengazo zinali zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 12:1

Uzikumbukanso Mlengi wako pa masiku a unyamata wako, masiku oipa asanafike, zisanafikenso zaka zoti uzidzati, “Moyowu wandikola.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 36:6

Kulungama kwanu kumaonekera ngati mapiri aatali, kuweruza kwanu nkozama ngati nyanja yakuya, Inu Chauta, mumasamalira anthu ndi nyama zomwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 43:7

Onsewo amadziŵika ndi dzina langa, ndidaŵalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndidaŵapanga ndi kuŵapatsa moyo.”

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:1

Pachiyambi Mulungu adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 11:3

Pokhala ndi chikhulupiriro timamvetsa kuti zonse zimene zilipo zidalengedwa ndi mau a Mulungu, mwakuti zinthu zoonekazi zidachokera ku zinthu zosaoneka.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:16

Kudzera mwa Iye Mulungu adalenga zonse zakumwamba ndi zapansipano, zooneka ndi zosaoneka, mafumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu ena onse. Mulungu adalenga zonse kudzera mwa Iye, zonsezo adalengera Iyeyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 2:7

Tsono Chauta adatenga dothi pa nthaka, ndipo adaumba munthu ndi dothilo. Adamuuzira mpweya wopatsa moyo m'mphuno zake, ndipo munthuyo adakhala wamoyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 4:11

“Inu Ambuye athu ndi Mulungu wathu, ndinu oyenera kulandira ulemerero, ulemu ndi mphamvu, pakuti ndinu mudalenga zinthu zonse. Mudafuna kuti zonsezo zikhalepo, ndipo zidalengedwa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 1:1-3

Pachiyambi pa zonse Iye amene amatchedwa dzina loti Mau, anali alipo kale. Anali kwa Mulungu, ndipo anali Mulungu.

Wotchedwa Mauyo anali m'dziko lapansi, ndipo Mulungu adalenga dziko lapansilo kudzera mwa Iye, komabe anthu apansipano sadamzindikire.

Adaabwera kwao ndithu, koma anthu ake omwe sadamlandire.

Komabe ena adaamlandira nakhulupirira dzina lake, ndipo ameneŵa Iye adaŵapatsa mphamvu zoti akhale ana a Mulungu.

Kukhala ana a Mulungu kumeneku sikudachokere m'kubadwa kwao, kapena ku chifuniro cha thupi, kapena ku chifuniro cha munthu ai, koma kudachokera kwa Mulungu.

Wotchedwa Mau uja adasanduka munthu, nadzakhala pakati pathu. Anali wokoma mtima ndi wokhulupirika kwabasi. Ndipotu tidaona ulemerero wake, ndiye kuti ulemerero womwe Iye amalandira kwa Atate pokhala Mwana wao mmodzi yekha uja.

Yohaneyo adaamchitira umboni. Ankauza anthu mwamphamvu kuti, “Uyu ndiye uja ndinkanenayu kuti amene akubwera pambuyo panga ngwoposa ine; pakuti ine ndisanabadwe, Iye alipo.”

Kuchokera m'kukoma mtima kwake kwathunthu ife tonse tidalandira madalitso, madalitso ake otsatanatsatana.

Paja Mulungu adatipatsa Malamulo ake kudzera mwa Mose, koma kudzera mwa Yesu Khristu adatizindikiritsa kukoma mtima ndi kukhulupirika kwake.

Chikhalire palibe munthu amene adaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekha uja, amene ali wapamtima wa Atate, ndiye adaulula za Mulunguyo.

Nthaŵi ina akuluakulu a Ayuda a ku Yerusalemu adaatuma ansembe ndi Alevi ena kukafunsa Yohane kuti, “Kodi iwe ndiwe yani?”

Anali kwa Mulungu chikhalire.

Iye adayankha mosabisa konse, adanenetsa ndithu kuti, “Inetu sindine Mpulumutsi wolonjezedwa uja ai.”

Adamufunsanso kuti, “Nanga ndiwe yani? Ndiwe Eliya kodi?” Iye adati, “Iyai, sindine Eliya.” Iwo adati, “Kodi ndiwe Mneneri tikumuyembekeza uja?” Koma Yohane adayankha kuti, “Ainso.”

Tsono adamuuza kuti, “Tanena zenizenitu, kuti tikaŵafotokozere bwino amene atituma. Mwiniwakewe umati ndiwe yani?”

Yohane adaŵayankha kuti, “Monga adaanenera mneneri Yesaya: “Ine ndine liwu la munthu wofuula m'chipululu; akunena kuti, ‘Ongolani mseu wodzadzeramo Ambuye.’ ”

Anthu aja adaaŵatuma ndi Afarisi.

Tsono adafunsa Yohane kuti, “Ngati sindiwe Mpulumutsi wolonjezedwa uja, kapena Eliya, kapenanso Mneneri tikumuyembekeza uja, nanga bwanji umabatiza?”

Yohane adaŵayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panupa pali wina amene inu simukumdziŵa.

Iyeyu ngwobwera pambuyo panga, komabe sindili woyenera ngakhale kumasula zingwe za nsapato zake.”

Zimenezi zidachitikira ku Betaniya, kutsidya kwa mtsinje wa Yordani, kumene Yohane ankabatiza.

M'maŵa mwake Yohane adaona Yesu akubwera kwa iye, ndipo adati, “Suuyu Mwanawankhosa wa Mulungu uja, wochotsa machimo a anthu a pa dziko lonse lapansi.

Mulungu adalenga zonse kudzera mwa Iye, ndipo palibe chilichonse chimene chidalengedwa popanda Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:20

Pajatu chilengedwere cha dziko lapansi anthu akhala akuzindikira makhalidwe osaoneka a Mulungu, ndiye kuti mphamvu zake zosatha, ndiponso umulungu wake. Akhala akuzizindikira poona zimene Mulungu adalenga. Choncho alibe konse pozembera.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 20:11

Paja pa masiku asanu ndi limodzi Chauta adalenga zonse zakumwamba, za pa dziko lapansi, nyanja ndi zinthu zonse zam'menemo, koma pa tsiku lachisanu ndi chiŵiri adapumula. Nchifukwa chake Chauta adadalitsa tsiku la Sabata, nalisandutsa loyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 12:7-9

“Koma ufunse kwa nyama zakuthengo, zidzakuphunzitsa. Ufunse mbalame zamumlengalenga, zidzakuuza.

Upemphe nzeru kwa zolengedwa za dziko lapansi, zidzakuphunzitsa, ngakhale nsomba zam'nyanja zidzakufotokozera.

Kodi mwa zonsezo nchiti chimene sichidziŵa kuti zonsezi adachita ndi Chauta?

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 1:10

Adatinso, “Inu Ambuye, ndinu amene mudalenga dziko lapansi pachiyambi pomwe, zakumwambaku ndi ntchito ya manja anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:26

Zitatha izo Mulungu adati, “Tiyeni tipange munthu m'chifanizo chathu, adzakhale wonga Ifeyo. Adzalamulire nsomba zam'nyanja, mbalame zamumlengalenga, nyama zoŵeta, ndi zokwaŵa zonse za pa dziko lapansi.”

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 3:5

Apa akuiŵala dala kuti kalelo Mulungu atanena mau, zakuthambo zidalengedwa, ndipo dziko lapansi lidapangidwa ndi madzi kufumira m'madzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 10:12

Chauta ndiye amene adalenga dziko lapansi ndi mphamvu zake. Ndiye amene adapanga zonse ndi nzeru zake ndipo ndi umisiri wake adayala thambo lakumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 11:36

Paja zinthu zonse nzochokera kwa Iye, nzolengedwa ndi Iye ndipo zimalinga kwa Iye. Ulemerero ukhale wake mpaka muyaya. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:6

Chauta adalankhula ndipo zakumwamba zidalengedwa. Zonse zakumeneko zidalengedwa pamene Iye adalankhula mau ake.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Atate wanga wachikondi komanso wolungama, ndinu mlengi wa moyo wanga, manja anu odzala ndi chikondi adapanga chilichonse cha ine, kupatsa tanthauzo zonse zomwe ndili. M'dzina la Yesu ndikubwera kwa inu, kukuthokozani chifukwa cha zodabwitsa zomwe manja anu alenga, ndinu wamphamvu, wangwiro komanso wabwino. Atate, kumwamba ndi kwanu, dziko lapansi ndi lanunso, dziko lonse ndi zake zonse, kumpoto ndi kum'mwera, inu munalizika. Ndinu Mulungu wosatha, mlengi wa malekezero a dziko lapansi, simutopa kapena kugwa mphwayi, ndipo nzeru zanu n'zosayesedwa. Ndikukweza dzina lanu Yesu Mwana wa Mulungu, pakuti, chifukwa cha inu zonse zinalengedwa ndipo chifukwa cha inu zikukhala, monga momwe zalembedwera: "Chifukwa cha iye, ndipo chifukwa cha iye, ndipo zonse zilipo. Ulemerero ukhale kwa iye nthawi zonse. Ameni. " Mzimu Woyera, ndi choonadi chanu ndi chitonthozo chanu dzudzitsani dziko lapansi m'chilungamo, uchimo ndi chiweruzo kuti liyende ku chikondi cha Atate, mverani kulira kwa chilengedwe, Mulungu wokondedwa ndipo muchitire chifundo ana anu, inu amene mumakhala kumwamba ndipo dziko lapansi ndi chopondapo mapazi anu, tsekani khutu lanu ndipo mutikhululukire machimo athu. Ndiphunzitseni kuona ukulu wanu kudzera m'chilengedwe, chilichonse chilichonse chomwe mumandipatsa, chomwe ndimakhala nacho ndikusangalala nacho chimandipangitsa kuganiza za inu chifukwa ndinu womwe mumandipatsa zonse, kuyambira mpweya womwe ndimapumira mpaka chakudya chomwe mumayika patebulo langa. Zikomo chifukwa cha zonse zomwe mudalenga kuti ndikhale woyamikira komanso wosangalala pamene ndili padziko lapansi. Mu dzina la Yesu, Ameni.