Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

MAVESI ODALITSA

Pali anthu apadera amene Mulungu waika pa moyo wako, ndi anthu odalitsidwa ndi okondedwa, amene tikuwadalitsa m'dzina la Yesu. M'Baibulo muli mavesi ambiri oti tithokoze ndi kudalitsa miyoyo imeneyi.

Sitimadalitsa anthu okhawo, koma mabanja athu, dziko lathu, ndi abale athu mwa Khristu. “Yehova akudalitse, nakusunge; Yehova akuunikire nkhope yake pa iwe, nakuchitire chifundo; Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatsenso mtendere.” (Numeri 6:24-26)

Timadalitsanso abusa athu amene Mulungu amawagwiritsa ntchito. “Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungama; Mudzam'zungulira ndi chiyanjo chanu ngati ndi chishango.” (Salimo 5:12)

Sitiyenera kudalitsa okhawo atichitira zabwino, chifukwa Mulungu watilamula kuti tizidalitsa ngakhale atichitira zoipa. “Dalitsani iwo akutikuzunzani; dalitsani, musatemberere.” (Aroma 12:14)


Masalimo 30:11-12

Mwasandutsa kulira kwanga kuti kukhale kuvina, mwachotsa chisoni changa ndi kundipatsa chisangalalo.

Choncho ndisakhale chete, koma ndikutamandeni ndi mtima wonse. Choncho mtima wanga udzakuimbirani mosalekeza, Chauta, Mulungu wanga, ndidzakuthokozani mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 101:1

Ndidzaimba nyimbo zotamanda kukhulupirika ndi kulungama. Ndidzakuimbirani Inu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 98:4-5

Fuulirani Chauta ndi chimwemwe, inu dziko lonse lapansi. Muimbireni mokondwa nyimbo zotamanda.

Imbani nyimbo zoyamika Chauta ndi pangwe, lizani pangwe ndi nyimbo zokoma.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:9

Imbirani Chauta, muimbireni nyimbo zomtamanda, lalikani za ntchito zake zodabwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 109:30

Ndidzathokoza Chauta kwambiri polankhula. Ndidzamtamanda pakati pa gulu la anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 47:1

Ombani m'manja inu anthu a mitundu yonse. Fuulani kwa Mulungu poimba nyimbo zachimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:24

Lero ndiye tsiku limene Chauta adalipanga. Tiyeni tikondwe ndi kusangalala pa tsiku limeneli.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:3

Koma anthu anu Mulungu, akondwere, asangalale pamaso panu, inde, asekere ndi chimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 34:22

Muzichita chikondwerero cha masabata, ndi chikondwerero cha kukolola tirigu woyambirira, ndi chikondwerero cha kututa zokolola zonse pakutha pake pa chaka.

Mutu    |  Mabaibulo
Numeri 29:12

“Pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiŵiri womwewo, muchite msonkhano wopatulika. Musagwire ntchito zotopetsa, ndipo muchite chikondwerero cholemekeza Chauta masiku asanu ndi aŵiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 12:14

“Tsiku limeneli muzidzalisunga. Tsiku limeneli muzidzalikumbukira, ndipo muzidzachita chikondwerero, kupembedza Chauta. Mibadwo yonse izidzakumbukira tsikuli, kuti likhale lamulo lamuyaya, lakuti muzidzachita chikondwerero pa tsiku limenelo.”

Mutu    |  Mabaibulo
Numeri 9:2

“Aisraele azichita Paska pa nthaŵi yake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 42:10

Imbirani Chauta nyimbo yatsopano. Mtamandeni, inu okhala m'dziko lonse lapansi! Mtamandeni, inu zolengedwa zonse zam'nyanja. Imbani, inu maiko akutali ndi onse okhala kumeneko.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:1

Tamandani Chauta! Nkwabwino kuimba nyimbo zotamanda Mulungu wathu, nkokondwetsa mtima kumtamanda moyenera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 48:1

Chauta ndi wamkulu, ndi woyenera kumutamanda kwambiri. Timuyamike mu mzinda wake, pa phiri lake loyera,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 66:8

Lemekezani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthunu, mau omtamanda Iye amveke.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 30:29

Koma inu anthu a Mulungu, mudzakondwa ndi kuimba monga m'mene mumachitira usiku pa chikondwerero chopatulika. Mudzasangalala ngati anthu opita naimba toliro ku phiri la Chauta, thanthwe la Israele.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:15

Mverani nyimbo m'mahema mwa anthu a Mulungu, nyimbo zokondwerera kupambana, zakuti, “Dzanja lamanja la Chauta limagonjetsa mwamphamvu,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 100:1-2

Fuulani kwa Chauta ndi chimwemwe, inu maiko onse.

Tumikirani Chauta mosangalala. Bwerani pamaso pake mukuimba mokondwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 148:13-14

Onsewo atamande dzina la Chauta, pakuti dzina lake lokha nlolemekezeka, ulemerero wake ndi woposa, pansi pano nkumwamba komwe.

Chauta wakweza anthu ake poŵapatsa mphamvu. Walemekeza anthu ake onse oyera mtima, Aisraele amene Iye amaŵakonda. Tamandani Chauta!

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 25:1

Inu Chauta, ndinu Mulungu wanga. Ndidzakulemekezani ndi kutamanda dzina lanu. Pakuti mwachita zinthu zodabwitsa mokhulupirika ndi motsimikiza, zinthu zimene mudakonzeratu kalekale.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 22:4

Ndimaitana Chauta, amene ayenera kumtamanda, ndipo amandipulumutsa kwa adani anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 75:9

Koma ine sindidzaleka kukondwera, ndidzaimba nyimbo zotamanda Mulungu wa Yakobe mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:3

Mulungu waika nyimbo yatsopano m'kamwa mwanga, nyimbo yake yotamanda Iye. Anthu ambiri adzaona zimenezi ndipo adzaopa, nadzakhulupirira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 150:1-6

Tamandani Chauta! Tamandani Mulungu m'malo ake opatulika. Mtamandeni ku thambo lake lamphamvu.

Mtamandeni chifukwa cha ntchito zake zamphamvu, mtamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.

Mtamandeni pomuimbira lipenga, mtamandeni ndi gitara ndi zeze.

Mtamandeni poimba ng'oma ndi povina, mtamandeni ndi zipangizo zansambo ndi mngoli.

Mtamandeni ndi ziwaya zamalipenga zolira, mtamandeni ndi ziwaya zamalipenga zolira kwambiri.

Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Chauta. Tamandani Chauta!

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:8

Thokozani Chauta, tamandani dzina lake, lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:25

Chauta ngwamkulu, ngwoyenera kumtamanda kwambiri, ngwoyenera kumuwopa kupambana milungu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 7:17

Ine ndidzathokoza Chauta chifukwa cha kulungama kwake, ndidzaimba nyimbo zotamanda dzina la Chauta, Wopambanazonse uja.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 135:1-3

Tamandani Chauta. Tamandani dzina la Chauta, Perekani matamando, inu atumiki a Chauta,

Ndiye amene adaononga mitundu yambiri ya anthu, ndi kupha mafumu amphamvu aja,

Sihoni, mfumu ya Aamori, ndi Ogi, mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi maufumu onse a ku Kanani.

Adapereka dziko lao kuti likhale choloŵa, choloŵa cha Aisraele, anthu ake.

Dzina lanu, Inu Chauta, nlamuyaya, kutchuka kwanu ndi kwa pa mibadwo yonse.

Pakuti Chauta adzaweruza anthu ake kuti alibe mlandu, adzachitira chifundo atumiki ake.

Mafano a mitundu ina ya anthu ndi asiliva ndi agolide chabe, ndi opangidwa ndi manja a anthu.

Pakamwa ali napo, koma salankhula, maso ali nawo, koma sapenya.

Makutu ali nawo, koma saamva, ndipo alibe mpweya m'kamwa mwao.

Anthu amene amapanga mafanowo afanefane nawo, chimodzimodzi onse amene amaŵakhulupirira.

Inu a m'banja la Israele, tamandani Chauta! Inu a m'banja la Aroni, tamandani Chauta!

inu amene mumatumikira m'Nyumba ya Chauta, m'mabwalo a Nyumba ya Mulungu wathu!

Inu a banja la Levi, tamandani Chauta! Inu amene mumaopa Chauta, tamandani Chauta!

Atamandike ku Ziyoni Chauta, amene amakhala ku Yerusalemu! Tamandani Chauta!

Tamandani Chauta, pakuti ngwabwino. Muimbireni nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nlokoma kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:171

Pakamwa panga padzakutamandani, chifukwa mumandiphunzitsa malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:21

Pakamwa panga padzayamika Chauta, zamoyo zonse zitamande dzina lake loyera mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 18:49

Chifukwa cha zimenezi ndidzakutamandani Inu Chauta, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzaimba nyimbo zotamanda dzina lanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:1-3

Bwerani, timuimbire Chauta. Tiyeni tifuule ndi chimwemwe kwa Iye, thanthwe lotipulumutsa.

Pa zaka makumi anai ndidaipidwa ndi mbadwo umenewo, choncho ndidati, “Ameneŵa ndi anthu osakhulupirika, sasamalako njira zanga.”

Choncho ndidakwiya nkulumbira kuti anthuwo sadzaloŵa ku malo anga ampumulo.

Tiyeni, tikafike pamaso pake, tikamthokoze, tiyeni tifuule kwa Iye ndi chimwemwe, timuimbire nyimbo zotamanda.

Pakuti Chauta ndiye Mulungu wamkulu, ndiye Mfumu yaikulu yopambana milungu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 69:30

Ndidzatamanda dzina la Mulungu pomuimbira nyimbo, ndidzalalika ukulu wake pomuthokoza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:19

Ndidzazipereka m'mabwalo a Nyumba ya Mulungu, mu mzinda wa Yerusalemu. Tamandani Chauta!

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:7

Adzasimba za ubwino wanu, adzaimba nyimbo zotamanda kulungama kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 81:1-3

Kwezani mau kuimbira Mulungu amene ali mphamvu zathu. Fuulani ndi chimwemwe kwa Mulungu wa Yakobe.

Ine ndine Chauta, Mulungu wanu, amene ndidakutulutsani m'dziko la Ejipito. Yasamani kukamwa, Ine ndidzakudyetsani.

“Koma anthu anga sadamvere mau anga. Israele adandinyoza.

Choncho ndidaŵasiya ndi mitima yao yosamverayo, kuti atsate zimene ankafuna.

“Anthu anga akadandimvera, Aisraele akadayenda m'njira zanga,

bwenzi posachedwa nditagonjetsa adani ao, ndipo dzanja langa likadakantha amaliwongo ao.

“Anthu amene amadana ndi Chauta, akadakhwinyata pamaso pake, ndipo tsoka lao likadakhala mpaka muyaya.

Ndikadakudyetsani ndi ufa wosalala watirigu, ndipo ndikadakukhutitsani ndi uchi wam'thanthwe.”

Yambani nyimbo, imbani ng'oma, pamodzi ndi pangwe wolira bwino ndi zeze.

Imbani lipenga mwezi ukaoneka chatsopano, ukaoneka kwathunthu, pa tsiku lathu lachikondwerero.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 47:6

Imbani nyimbo zotamanda Mulungu, imbani nyimbo zotamanda. Imbani nyimbo zotamanda mfumu yathu, imbani nyimbo zotamanda.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:32

Imbirani Mulungu nyimbo, inu maufumu a pa dziko lapansi. Imbani nyimbo zotamanda Ambuye,

Mutu    |  Mabaibulo
Nehemiya 8:10

Tsono Nehemiya adapitiriza nati, “Kazipitani, mukachite phwando ku nyumba, kenaka muŵapatseko anzanu amene sadakonze kanthu. Pakuti lero ndi tsiku loyera kwa Chauta, Mulungu wathu. Tsono musakhale ndi chisoni, popeza kuti chimwemwe chimene Chauta amakupatsani, chimakulimbikitsani.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:2

Tiyeni, tikafike pamaso pake, tikamthokoze, tiyeni tifuule kwa Iye ndi chimwemwe, timuimbire nyimbo zotamanda.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 126:3

Ndithudi, Chauta watichitira zazikulu, ndipo tasangalala.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 12:4-6

Tsiku limenelo mudzati: “Thokozani Chauta, tamandani dzina lake. Mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.

“Imbirani Chauta nyimbo zotamanda, pakuti wachita zazikulu. Zimenezi zidziŵike pa dziko lonse lapansi.

Fuulani ndi kuimba mokondwa, inu anthu a ku Ziyoni, pakuti Woyera Uja wa Israele ndi wamkulu pakati panu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:3

Lalikani pamodzi nane ukulu wa Chauta, tiyeni limodzi tiyamike dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:23-31

Imbirani Chauta, inu anthu a dziko lonse lapansi. Lengezani tsiku ndi tsiku za m'mene Iye adapulumutsira anthu ake.

Lalikani za ulemerero wake kwa anthu a mitundu yonse, simbani za ntchito zake zodabwitsa kwa anthu a m'maiko onse.

Chauta ngwamkulu, ngwoyenera kumtamanda kwambiri, ngwoyenera kumuwopa kupambana milungu yonse.

Paja milungu ya anthu a mitundu ina ndi mafano chabe, koma Chauta ndiye adalenga zakumwamba.

Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi chimwemwe zili m'Nyumba mwake.

Tamandani Chauta, inu anthu a mitundu yonse, vomerezani kuti ulemerero ndi mphamvu, zonse nza Chauta.

Tamandani ulemerero wa dzina la Chauta. Bwerani ndi zopereka, ndipo muloŵe m'mabwalo a Nyumba yake. Pembedzani Chauta waulemerero ndi woyera.

Kenaka adagaŵira Aisraele onsewo, amuna ndi akazi, aliyense mtanda wa buledi, nthuli ya nyama ndiponso keke ya mphesa zouma.

Njenjemerani pamaso pake, inu anthu onse a pa dziko lapansi. Ndithu dziko lapansi lakhazikika kolimba, osatha kuligwedeza.

Zakumwamba zisangalale, za pansi pano zikondwere, zonsezo zilengeze kwa anthu onse kuti, “Chauta ndiye mfumu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 50:14

“Koma perekani nsembe zanu zothokozera kwa Mulungu, ndipo muchite zimene mudalumbira kwa Wopambanazonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Nehemiya 12:27

Pamene anthu adati apereke kwa Mulungu khoma lozinga mzinda wa Yerusalemu, adaitana Alevi kuchokera konse kumene ankakhala, kuti abwere ku Yerusalemu kudzachita mwambo wopereka khomalo mokondwera, mothokoza ndiponso poimba pamodzi ndi ziwaya zamalipenga, azeze ndi mapangwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:19

Muzichezerana ndi mau a masalimo ndi a nyimbo za Mulungu ndi zauzimu. Ndipo muziimbira Ambuye mopolokezana ndi mtima wanu wonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:16

Mau a Khristu akhazikike kwathunthu m'mitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana ndi nzeru zonse. Muziimbira Mulungu ndi chiyamiko m'mitima mwanu, pamene mukuimba masalimo, nyimbo zotamanda Mulungu ndi nyimbo zina zauzimu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 149:1-3

Tamandani Chauta! Imbirani Chauta nyimbo yatsopano, imbani nyimbo yomtamanda pa msonkhano wa anthu ake oyera mtima.

Aisraele asangalale ndi Mlengi wao. Anthu a Ziyoni akondwere ndi Mfumu yao.

Atamande dzina lake povina, amuimbire nyimbo yokoma ndi ng'oma ndi pangwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 9:9

Kondwani kwambiri, inu anthu a ku Ziyoni. Fuulani kwambiri, inu anthu a ku Yerusalemu. Onani, mfumu yanu ikudza kwa inu. Ikubwera ili yopambana ndi yogonjetsa adani. Ndi yodzichepetsa ndipo yakwera pa bulu, bulu wake kamwana tsono.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 19:37-40

Pamene ankayandikira Yerusalemu, pa matsitso a Phiri la Olivi, gulu lonse la omutsatira aja lidayamba kukondwerera. Adakweza mau, natamanda Mulungu chifukwa cha ntchito zonse zamphamvu zimene iwo adaziwona.

Adati, “Ndi yodala Mfumu imene ilikudza m'dzina la Ambuye. Mtendere Kumwamba, ulemu kwa Mulungu kumwambamwamba.”

Apo Afarisi ena amene adaali m'khamumo adauza Yesu kuti, “Aphunzitsi, auzeni ophunzira anuŵa aleke zimenezi.”

Tsono adathamangira kutsogolo, nakakwera mu mkuyu kuti amuwone, chifukwa Yesu ankayenera kudzera pamenepo.

Iye adati, “Ndikutitu iwoŵa akangokhala chete, ifuula ndi miyalayi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 9:1-2

Ndidzakuthokozani, Inu Chauta, ndi mtima wanga wonse. Ndidzasimba za ntchito zanu zonse zodabwitsa.

Amene amadziŵa dzina lanu, Inu Chauta, amakukhulupirirani, pakuti Inu Chauta simuŵasiya anthu okufunitsitsani.

Imbani nyimbo zotamanda Chauta amene amakhala ku Ziyoni. Lalikani za ntchito zake kwa anthu a mitundu yonse.

Paja Iye amachitira chifundo anthu ozunzika, salephera kumva kulira kwao ndipo amalanga anthu oŵazunzawo.

Mundikomere mtima, Inu Chauta. Onani m'mene akundisautsira anthu ondida. Inu mumandipulumutsa ku imfa,

kuti ndithe kuyamika ntchito zanu zonse, pakati pa anthu anu a mu Ziyoni. Zoonadi ndidzakondwa chifukwa mwandipulumutsa.

Akunja agwera m'mbuna yokumba iwo omwe. Phazi lao lakodwa mu ukonde wobisika wotcha iwo omwe.

Chauta wadziwulula yekha, pakuweruza molungama, koma anthu oipa akodwa mu msampha wotcha iwo omwe.

Tsono anthu oipa adzapita ku dziko la anthu akufa, ndiye kuti anthu onse amene amakana Mulungu.

Koma anthu aumphaŵi Mulungu saŵaiŵala nthaŵi zonse, anthu osauka Mulungu saŵagwiritsa mwala mpang'ono pomwe.

Dzambatukani, Inu Chauta, munthu asakunyozeni. Azengeni mlandu anthu akunja.

Ndidzakondwa ndi kusangalala chifukwa cha Inu, ndidzaimba nyimbo zotamanda dzina lanu, Inu Wopambanazonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:1-3

Ndidzayamika Chauta nthaŵi zonse, pakamwa panga padzatamanda Iye kosalekeza.

Ngakhale anaamkango amasoŵa chakudya ndipo amakhala anjala, koma anthu amene amalakalaka Chauta, sasoŵa zinthu zabwino.

Bwerani ana anga, mundimvere, ndidzakuphunzitsani kuwopa Chauta.

Ndani mwa inu amakhumba moyo ndi kulakalaka kuti akhale masiku ambiri, kuti asangalale ndi zinthu zabwino?

Ngati ufunadi moyo, usalankhule zoipa, pakamwa pako pasakambe zonyenga.

Lewa zoipa, ndipo uchite zabwino. Funafuna mtendere ndi kuulondola.

Ngati mumvera Chauta, adzakuyang'anirani ndipo adzayankha kupempha kwanu.

Koma Chauta amaŵakwiyira anthu ochita zoipa, anthuwo sadzakumbukikanso pansi pano.

Pamene anthu ake akulira kuti aŵathandize, Chauta amamva naŵapulumutsa m'mavuto ao onse.

Chauta amakhala pafupi ndi anthu a mtima wosweka, amapulumutsa otaya mtima.

Anthu a Mulungu amaona masautso ambiri. Komabe Chauta amawapulumutsa m'mavuto awo onse.

Moyo wanga umanyadira Chauta. Anthu ozunzika amve ndipo akondwere.

Chauta amasunga thupi la munthuyo, palibe fupa limene limasweka.

Choipa chitsata mwini, anthu odana ndi munthu wa Mulungu adzalangidwa.

Chauta amaombola moyo wa atumiki ake. Palibe wothaŵira kwa Iye amene adzalangidwe.

Lalikani pamodzi nane ukulu wa Chauta, tiyeni limodzi tiyamike dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:1-2

Tsono abale, popeza kuti Mulungu watichitira chifundo chachikulu chotere, ndikukupemphani kuti mupereke matupi anu omwe kuti akhale nsembe yamoyo, yopatulika, ndi yokondwetsa Mulungu. Imeneyi ikhale njira yanu yopembedzera Mulungu mwauzimu.

Muzikondana kwenikweni monga abale, ndipo muzichita ngati kupikisana poonetsana ulemu.

Potumikira Ambuye, changu chanu chisazilale, koma chikhalebe choyaka.

Muzikhala okondwa chifukwa cha chiyembekezo chanu. Muzipirira pakati pa masautso, ndipo muzipemphera nthaŵi zonse.

Muzipereka zothandiza akhristu anzanu osoŵa, ndipo muziyesetsa kulandira alendo mokondwa.

Pemphani Mulungu kuti aŵadalitse amene amakuzunzani. Ndithu, pemphani kuti aŵadalitse, osaŵatemberera ai.

Muzikondwa nawo amene akukondwa, muzilira nawo amene akulira.

Muzimvana bwino, ndipo musamadzikweze, koma muziyanjana nawo anthu wamba. Musamadziyese anzeru.

Munthu akakuchitani choipa, musamubwezere choipa. Yesani kuchita zimene anthu onse amaziwona kuti nzabwino.

Ngati nkotheka, khalani ndi mtendere ndi anthu onse, monga momwe mungathere.

Okondedwa anga, musabwezere choipa, koma alekeni, mkwiyo wa Mulungu ndiwo uŵalange. Paja Malembo akuti, “Kulipsira nkwanga. Ndidzaŵalanga ndine, akutero Chauta.”

Musamatsanzira makhalidwe a anthu odalira zapansipano, koma Mulungu asinthe moyo wanu wonse pakukupatsani mitima yatsopano. Pamenepo mudzatha kudziŵa zimene Mulungu afuna, ndipo mudzazindikira zimene zili zabwino, zangwiro ndi zomkondwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 42:4

Mtima wanga umaŵawa ndikamakumbukira m'mene ndinkayendera ndi chinamtindi cha anthu, poŵatsogolera ku Nyumba ya Mulungu. Panali khwimbi la anthu ofuula mosangalala, akuimba nyimbo zothokoza ndipo akuchita chikondwerero.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:30

Tsono ataimba nyimbo yotamanda Mulungu, onse adatuluka nkumapita ku Phiri la Olivi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:9

Koma inu ndinu fuko losankhidwa, ansembe achifumu, mtundu wopatulika, anthu akeake a Mulungu. Adakusankhani kuti mukalalike ntchito zamphamvu za Iye amene adakuitanani kuti mutuluke mu mdima, mukaloŵe m'kuŵala kwake kodabwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:15

Nchifukwa chake, kudzera mwa Yesu tiyeni tipereke kosalekeza mayamiko athu kwa Mulungu ngati nsembe. Ndiye kunena kuti tipereke ngati nsembe mau athu ovomereza dzina lake poyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 66:1-4

Tamandani Mulungu ndi chimwemwe mokweza mau, inu anthu onse a pa dziko lapansi.

Inu Mulungu, mwatiyesa, mwatiyeretsa monga m'mene amayeretsera siliva.

Inu mudatiloŵetsa mu ukonde wa adani, mudatisenzetsa katundu wolemera pamsana pathu.

Inu mudalola kuti adani atikwere pa mutu, tidaloŵa m'moto ndiponso m'madzi, komabe Inu mwatifikitsa ku malo opulumukirako.

Ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza, ndidzachitadi zimene ndidazilumbira kwa Inu,

zimene ndidalankhula ndi pakamwa panga, ndiponso zimene ndidalonjeza pamene ndinali pa mavuto.

Ndidzapereka kwa Inu nsembe zopsereza za nyama zonenepa, utsi wa nsembe za nkhosa zamphongo udzafika kwa Inu. Ndidzaperekanso ngati nsembe ng'ombe zamphongo ndi mbuzi.

Bwerani mudzamve, inu nonse amene opembedza Mulungu, ndidzakusimbireni zimene Iye wandichitira.

Ndidafuula kwa Iye, ndipo ndidamtamanda ndi pakamwa panga.

Ndikadazindikira choipa chilichonse mumtima mwanga ndi kuchibisa, Ambuye sakadandimvera.

Koma zoonadi, Mulungu wandimvera, wasamala mau a pemphero langa.

Imbani nyimbo zoyamika dzina lake laulemerero, mumtamande mwaulemu.

Mulungu atamandike chifukwa sadakane pemphero langa, sadachotse chikondi chake chosasinthika kwa Ine.

Muuzeni Mulungu kuti, “Ntchito zanu nzodabwitsa kwambiri. Mphamvu zanu nzazikulu, kotero kuti adani anu amakuŵeramirani moopa.

Anthu onse a pa dziko lapansi amakupembedzani, amaimba nyimbo zotamanda Inu, amaimba nyimbo zotamanda dzina lanu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 96:1-3

Imbirani Chauta nyimbo yatsopano! Imbirani Chauta, anthu a m'dziko lonse lapansi!

Uzani mitundu ya anthu kuti, “Chauta ndiye Mfumu. Dziko lonse lidakhazikitsidwa molimba, silidzagwedezeka konse. Adzaweruza mitundu yonse ya anthu mwachilungamo.”

Zakumwamba zisangalale, zapansi pano zikondwere, nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zam'menemo.

Minda zikondwe pamodzi ndi zonse zam'menemo. Mitengo yam'nkhalango idzaimba mokondwa

pamaso pa Chauta, pamene zabwera kudzalamulira dziko lapansi. Adzalamulira dziko lonse mwachilungamo, adzalamulira anthu a mitundu yonse moona.

Imbirani Chauta, tamandani dzina lake! Lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

Lengezani za ulemerero wake kwa anthu a mitundu yonse, simbani za ntchito zake zodabwitsa kwa anthu a m'maiko onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 71:23

Pakamwa panga padzafuula ndi chimwemwe, pamene ndikukuimbirani nyimbo zotamanda. Nawonso mtima wanga umene mwauwombola, udzaimba moyamika.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:1-2

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga, moyo wanga wonse umuyamike potchula dzina lake loyera.

Satilanga moyenerera machimo athu, satibwezera molingana ndi zolakwa zathu.

Monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, ndi momwenso chidakulira chikondi chake chosasinthika kwa anthu oopa Chauta.

Monga kuvuma kuli kutali ndi kuzambwe, ndi momwenso amachotsera zolakwa zathu kuti zikhale kutali ndi ife.

Monga bambo amachitira chifundo ana ake, ndi momwenso Chauta amaŵachitira chifundo omulemekeza.

Amadziŵa m'mene adatipangira, amakumbukira kuti ife ndife fumbi.

Kunena za munthu, masiku ake sakhalitsa, ali ngati a udzu, munthuyo amakondwa ngati duŵa lakuthengo.

Koma mphepo ikaombapo, duŵalo pamakhala palibe, siliwonekanso pa malo ake.

Koma chikondi cha Chauta nchamuyaya kwa anthu omumvera, zidzukulu zao zonse amazichitira zolungama.

Anthuwo ndi amene amasunga chipangano chake, amene amakumbukira kusunga malamulo ake.

Chauta wakhazikitsa mpando wake wachifumu kumwamba, ndipo amalamulira zonse mu ufumu wake.

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga, ndipo usaiŵale zabwino zake zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:11

Koma onse othaŵira kwa Inu akondwere, aziimba ndi chimwemwe nthaŵi zonse. Inu muŵatchinjirize, kuti okukondani akondwere chifukwa cha chitetezo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 15:1-2

Tsono Mose pamodzi ndi Aisraele aja adaimba nyimbo iyi, kuimbira Chauta, adati, “Ndidzaimbira Chauta chifukwa choti wapambana, waponya m'nyanja akavalo pamodzi ndi okwerapo omwe.

Koma Inu mudangouzira ndi mphepo yanu, ndipo nyanja idaŵamiza. Adangomira ngati chitsulo mpaka pansi pa madzi.

“Inu Chauta, kodi pali mulungu wina wofanafana nanu? Ndani amafanafana ndi Inu, amene muli aulemu chifukwa cha ungwiro wanu? Ndani amafanafana nanu, Inu amene muli oopsa chifukwa cha ntchito zanu zaulemu ndi zodabwitsa?

Mudatambalitsa dzanja lanu lamanja, ndipo nthaka idaŵameza.

“Koma anthu amene mudaŵaombola, mudaŵatsogolera ndi chikondi chanu chosasinthika. Mudaŵatsogolera ku malo anu oyera ndi mphamvu zanu.

Anthu a mitundu ina amva mbiriyi, ndipo anjenjemera ndi mantha. Mantha oopsa aŵagwira Afilisti.

Tsopano lino mafumu a ku Edomu ataya mtima. Atsogoleri a ku Mowabu ayambapo kunjenjemera. Onse a ku Kanani agooka m'nkhongono.

Onsewo agwidwa ndi mantha oopsa. Iwo akhala chete ngati mwala, chifukwa cha kuwopa mphamvu zanu zazikulu. Angokhala chete mpaka anthu anu, Inu Chauta, atabzola, anthu amene mudaŵaombola mu ukapolo.

Mudzaŵaloŵetsa ndi kuŵakhazika pa phiri lanu, pa malo amene Inu Chauta mudaŵapanga kuti akhale anu, m'nyumba yopembedzera imene Inu mudaimanga.

Chauta adzakhala mfumu mpaka muyaya.”

Pamene akavalo a Farao, pamodzi ndi magaleta ndi okwerapo ake omwe, adaloŵa m'nyanja, Chauta adaŵabweza madziwo, ndipo adamiza onsewo. Koma Aisraele adayenda pouma m'kati mwa nyanjayo.

Chauta ndiye mphamvu zanga, ndiye amene ndimamuimbira, ndiye chipulumutso changa. Iye ndiye Mulungu wanga, ndipo ndidzamtamanda. Ndiye Mulungu wa atate anga, ndipo ndidzamuyamika kwakukulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:7-9

Imbirani Chauta mothokoza, imbirani Mulungu wathu nyimbo yokoma ndi pangwe.

Amaphimba zakumwamba ndi mitambo, amapatsa nthaka mvula, amameretsa udzu pa magomo.

Amapereka chakudya kwa nyama ndi kwa ana a khungubwi pamene akulira chakudya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:1-2

Malo amene mumakhalamo, Inu Chauta Wamphamvuzonse, ndi okoma kwambiri.

Kukhala tsiku limodzi m'mabwalo anu nkwabwino kwambiri kupambana kukhala masiku ambiri kwina kulikonse. Nkadakonda kukhala wapakhomo wa Nyumba ya Mulungu wanga kupambana kukhala m'nyumba za anthu oipa.

Pakuti Chauta ndiye dzuŵa ndi chishango, amatichitira chifundo ndi kutipatsa ulemu. Chauta saŵamana zabwino anthu oyenda molungama.

Inu Chauta Wamphamvuzonse, ngwodala munthu woika chikhulupiriro chake pa Inu.

Mtima wanga ukulakalaka, mpaka kukomoka, kufunitsitsa kuwona mabwalo a Chauta. Inu Mulungu wamoyo, ndikukuimbirani mwachimwemwe ndi mtima wanga wonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 146:1-2

Tamandani Chauta! Tamanda Chauta, iwe mtima wanga.

Chauta adzakhala mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako, iwe Ziyoni, adzalamulira ku mibadwo yonse. Tamandani Chauta!

Ndidzatamanda Chauta pa moyo wanga wonse. Ndidzaimba nyimbo zotamanda Mulungu wanga nthaŵi zonse pamene ndili moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 138:1-2

Ndikukuthokozani Inu Chauta ndi mtima wanga wonse. Ndikuimba nyimbo zokutamandani pamaso pa milungu.

Ndikugwada moŵerama kumaso kwa Nyumba yanu yoyera. Ndikutamanda dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika, chifukwanso cha kukhulupirika kwanu. Mwakweza dzina lanu ndiponso malonjezo anu kupambana chinthu china chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 9:11

Imbani nyimbo zotamanda Chauta amene amakhala ku Ziyoni. Lalikani za ntchito zake kwa anthu a mitundu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:5-7

Ndidzasinkhasinkha za ulemerero ndi za ufumu wanu waukulu, ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.

Anthu adzasimba za mphamvu zanu zoopsa, inenso ndidzalalika za ukulu wanu.

Adzasimba za ubwino wanu, adzaimba nyimbo zotamanda kulungama kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 61:3

Wandituma kuti ndiŵakonzere zofunika olira a ku Ziyoni, ndiye kuti ndiŵapatse maluŵa achisangalalo m'malo mwa phulusa lachisoni, ndiŵapatse mafuta osonyeza kukondwa m'malo mwa kulira, ndiŵapatse chovala cha chikondwerero m'malo mwa kutaya mtima. Tsono adzatchedwa mitengo yamphamvu yachilungamo, yoibzala Chauta, kuti Iye mwini apezepo ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mbiri 5:13-14

Ndipo ntchito ya anthu oimba malipengawo ndi ya anthu oimba nyimbo aja, inali yakuti azimveketsa mau amodzi potamanda ndi kuthokoza Chauta, ndipo ankaimba nyimboyo ndi kuliza malipenga, ziwaya zamalipenga ndiponso zoimbira zina, kutamanda Chauta ndi mau akuti, “Ndithu Chauta ndi wabwino, pakuti chikondi chake chosasinthika chimakhala mpaka muyaya.” Apo Nyumbayo, Nyumba ya Chauta, idadzaza ndi mtambo,

ndipo ansembe sankatha kuimirira kuti agwire ntchito yao yotumikira, chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Chauta unali utadzaza m'Nyumba ya Chautayo.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye, inu ndinu Alfa ndi Omega! Atate, Mlengi wa thambo ndi dziko lapansi, ndinu woyamba ndi wotsiriza, chiyambi ndi chitsiriziro. Ndikubwera kwa inu kudzera mwa Ambuye wanga Yesu Khristu, ndikupempha kuti muteteze ndi kulimbitsa moyo wa mnzanga, mupatseni nzeru ndi luntha kuti asankhe zinthu zabwino, kuti ayende m'cholinga chimene munamupangira. Mulimbitseni, mutsitsimutseni mphamvu zake ndipo molimbikira mulimbitse chikhulupiriro chake, kotero kuti kukhalapo kwa Mzimu Woyera wanu kukhale patsogolo pa moyo wake ndi banja lake. Mawu anu amati: "Pakuti adzatumiza angelo ake kukutetezani m'njira zako zonse." Ambuye, pitirizani kumupatsa zonse zomfunika, mupatseni nzeru ndi kulimba mtima kuti agonjetse mantha ake ndipo athe kupambana mavuto aliwonse omwe akukumana nawo. Ndikulengeza kuti mukupita patsogolo pake ngati chimphona champhamvu, mukulimbana nkhondo zake zonse. Mumuteteze ku ziwembu zonse ndi misampha ya mdani. Zikomo, Ambuye, ulemerero ndi ulemu zonse zikhale kwa inu. M'dzina la Yesu. Ameni!