Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

NDIME ZA JOY

Chimwemwe cha Ambuye sichingondilimbitsa ine ndekha ayi, komanso chimatipangitsa kukhala ogwirizana. Chimwemwechi sichiyenera kubisika ayi, chiyenera kugawidwa. Monga momwe Aisraeli analangizidwira kusangalala ndikugawana zomwe anali nazo, inenso ndi iwe tiyenera kufalitsa chimwemwe cha Ambuye kwa anthu omwe timawadziwa.

Chimwemwe cha Ambuye chimandilimbikitsa kukonda anzanga ndikuwafikitsa uthenga wabwino. Tikakhala ndi mtima wosangalala mwa Mulungu, timakhala olimba mtima ndipo timatha kufalitsa chimwemwechi m'dera lathu.

Chimwemwe cha Mulungu ndi chosatha ndipo palibe angachichotse. Masalimo 98:4-6 amati: “Imbirani Ambuye, anthu onse a dziko lapansi! Yambani nyimbo zotamanda! Imbani ndi kuseŵera zeze! Imbirani Ambuye ndi zeze, ndi nyimbo zoyamika! Lizani malipenga ndi makonkereti, imbirani mfumu, Ambuye!” Apa mupeza mavesi ambiri onena za chimwemwe cha Mulungu wathu.


Genesis 12:2

Ndidzakusandutsa kholo la mtundu waukulu, ndipo ndidzakudalitsa ndi kukusandutsa wotchuka, kotero kuti udzakhala ngati dalitso kwa anthu ena.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 31:23

Chauta Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israele, akunena kuti, “Pamene ndidzabwezeranso anthu ufulu, kudzamvekanso mau ku dziko la Yuda ndi ku mizinda yake. Mau ake adzakhala akuti, ‘Chauta akudalitse iwe malo achilungamo, ndiponso iwe phiri loyera.’

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 19:24

Tsiku limenelo Israele adzakhala pamodzi ndi Ejipito ndi Asiriya, ndipo maiko atatuwo adzakhala dalitso pa dziko lonse lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 7:13

Adzakukondani ndi kukudalitsani, kotero kuti mudzachuluka ndi kubereka ana ambiri. Minda yanu adzaidalitsa, kotero kuti tirigu, vinyo ndi mafuta, mudzakhala nazo zonsezo. Adzakudalitsaninso pa zoŵeta pokupatsani ng'ombe zambiri ndi zoŵeta zina zomwe. Madalitso onseŵa, adzakupatsani muli m'dziko limene adalonjeza makolo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 9:22

Tsono Aroni adakweza manja ake pa Aisraele naŵadalitsa. Ndipo adatsika paguwa, pomwe adaperekera nsembe yopepesera machimo, nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 26:3

Khala kuno ndipo Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakudalitsa chifukwa ndidzapereka maiko onseŵa kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako. Ndidzasunga lumbiro limene ndidachita kwa bambo wako Abrahamu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 48:20

Motero adaŵadalitsa pa tsiku limenelo ndi mau akuti, “Aisraele adzatchula maina anu podalitsa. Adzanena kuti, ‘Mulungu akudalitseni inu monga Efuremu ndi Manase.’ ” Mwa njira imeneyi adaika Efuremu patsogolo pa Manase.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 12:3

“Ndidzadalitsa onse okudalitsa iwe, koma ndidzatemberera aliyense wokutemberera. Mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzapeza madalitso kudzera mwa iwe.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 61:9

Ana ao adzakhala odziŵika pakati pa anthu a mitundu ina, zidzukulu zaonso zidzakhala zotchuka pakati pa anthu onse. Aliyense woŵaona adzazindikira kuti ndi anthu amene Ine Chauta ndidaŵadalitsa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 49:25

Ndi Mulungu wa atate ako amene amakuthandiza, ndi Mulungu Mphambe amene amakudalitsa. Amakudalitsa ndi mvula yochokera mu mlengalenga, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo adzakudalitsa pakukupatsa ana ambiri ndi ng'ombe zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 30:16

Mukamamvera malamulo a Chauta, Mulungu wanu, ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero, mukamamkonda Chauta, Mulungu wanu ndi kutsata mau ake onse, pamenepo mudzakhala pabwino ndipo mudzakhala mtundu wa anthu ochuluka. Chauta, Mulungu wanu, adzakudalitsani m'dziko mukukakhalamolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 122:6

Pemphererani mtendere wa Yerusalemu ponena kuti, “Anthu amene amakukonda iwe Yerusalemu, zinthu ziziŵayendera bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:1-2

“Atonthozeni mtima, atonthozeni mtima anthu anga,” akutero Mulungu wanu.

Zoonadi, Ambuye Chauta akubwera kudzaweruza mwamphamvu, ndipo akulamulira ndi dzanja lake. Akubwera ndi malipiro ake, watsogoza mphotho yake.

Adzasamala nkhosa zake ngati mbusa. Adzasonkhanitsa anaankhosa ndi kuŵakumbatira. Ndipo adzatsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.

Kodi ndani adayesa kuchuluka kwa madzi am'nyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyesa kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani adayesa dothi lonse la dziko lapansi ndi dengu? Ndani adayesa kulemera kwa mapiri ndi magomo pa sikelo?

Ndani adalamulirapo maganizo a Chauta? Ndani adamphunzitsapo kanthu ngati mlangizi wake?

Kodi Chauta adapemphapo nzeru kwa yani, kuti adziŵe zinthu? Ndani adamuphunzitsa kuweruza molungama? Ndani adamphunzitsa kudziŵa zinthu? Ndani adamlangiza njira ya kumvetsa zinthu?

Mitundu ya anthu ili ngati kadontho ka madzi mu mtsuko, ilinso ngati fumbi chabe pa sikelo. M'manja mwa Chauta zilumba nzopepuka ngati fumbi.

Nkhalango ya ku Lebanoni siingakwanitse nkhuni zosonkhera moto, nyama zam'menemo sizingakwanire kuperekera nsembe yootcha.

Mitundu yonse ya anthu si kanthu konse pamaso pa Chauta, Iye amaziyesa zachabe ndi zopandapake.

Kodi Mulungu mungathe kumuyerekeza ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?

Likakhala fano, ndi munthu waluso amene amalipanga, kenaka mmisiri wa golide amalikuta ndi golide, nalipangira ukufu wasiliva.

“Muŵalankhule mofatsa anthu a ku Yerusalemu. Muŵauze kuti nthaŵi ya mavuto ao yatha, machimo ao akhululukidwa. Ndaŵalanga moŵirikiza chifukwa cha machimo ao.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:1

“Atonthozeni mtima, atonthozeni mtima anthu anga,” akutero Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 39:5

Kuyambira nthaŵi imene Yosefe adayamba kusamalira zonse za m'nyumba ya Potifarayo, Chauta adadalitsa zonse za kunyumba kwa Mwejipitoyo, ngakhale za kuminda kwake, chifukwa cha Yosefeyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 8:13

Inu mabanja a Yuda ndi Israele, kale munali chizindikiro cha matemberero pakati pa mitundu ina ya anthu. Koma tsopano ndidzakupulumutsani ndipo mudzakhala chizindikiro cha madalitso. Musaope, limbani mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 29:11

Chauta amapatsa anthu ake mphamvu. Amaŵadalitsa anthu ndi mtendere. Salmo la Davide. Nyimbo yoimba potsekula Nyumba ya Mulungu

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 125:1-2

Anthu amene amakhulupirira Chauta ndi olimba ngati phiri la Ziyoni, limene silingathe kugwedezeka, koma ndi lokhala mpaka muyaya.

Monga momwe mapiri amazingira Yerusalemu, momwemonso Chauta akuzinga anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 7:15

Chauta adzakutchinjirizani pa matenda onse. Iye sadzalolanso kuti matenda oopsa a ku Ejipito amene mumaŵadziŵa aja, afikenso pa inu, koma Mulungu adzadzetsa matenda ameneŵa pa adani anu onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 72:18-19

Atamandike Chauta, Mulungu wa Israele. Iye yekha ndiye amene amachita zinthu zodabwitsa.

Dzina lake laulemerero litamandike mpaka muyaya. Ulemerero wake udzaze dziko lonse lapansi. Inde momwemo. Inde momwemo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 55:5

Tsopano mudzaitana mitundu imene simuidziŵa. Mitundu imene sikudziŵani idzabwera ndi liŵiro kuti ikhale nanu, chifukwa cha Ine Chauta, Mulungu wanu, Woyera uja wa Israele, amene ndidakupatsani ulemerero.”

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 28:7

Chauta adzakuthandizani kuti mugonjetse adani anu pamene akuukirani. Pokuukirani adzatulukira njira imodzi, koma pothaŵa adzathaŵira m'zikuŵa zisanu ndi ziŵiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:27

Inde unali ufulu kuchita zimenezi, komanso unali udindo wao kuthandiza osaukawo. Ayuda adagaŵana madalitso ao achikhristu ndi anthu a mitundu ina, choncho iwowo ayeneranso kuthandiza Ayudawo pa zosoŵa zao za moyo wathupi.

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 2:8

Aliyense wokantha inu, wakantha chinthu cha mtengo wapatali zedi kwa Ine.” Tsono Chauta Wamphamvuzonse adandituma kwa mitundu imene idaagwira anthu ake kukaiwuza uthenga wake wakuti,

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 3:8

Koma Malembo adaoneratu kuti anthu a mitundu ina pakukhulupirira, Mulungu adzaŵaona kuti ngolungama pamaso pake. Nchifukwa chake Malembowo adaauziratu Abrahamu Uthenga Wabwinowu wakuti, “Mwa iwe Mulungu adzadalitsa anthu a mitundu yonse.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 137:5-6

Ndikakuiŵala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liwume.

Lilime langa likangamire ku mnakanaka m'kamwa mwanga, ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu ndi kukuwona kuti ndiwe wondisangalatsa kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 30:30

Kale munali ndi zoŵeta pang'ono koma tsopano zachuluka, ndipo Chauta wakudalitsani chifukwa cha ine. Tsopano ndiyenera kusamala banja langa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 54:10

Mapiri angathe kusuntha, magomo angathe kugwedezeka, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Lonjezo langa losunga mtendere mpaka muyaya silidzatha,” akuterotu Chauta amene amakumvera chifundo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 115:12-13

Chauta watikumbukira ndipo adzatidalitsa. Adzadalitsa anthu a Israele, adzadalitsa banja la Aroni.

Adzadalitsa amene amamlemekeza, anthu wamba ndi apamwamba omwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 3:8

Mumatipulumutsa ndinu, Inu Chauta. Madalitso anu akhale pa anthu anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 22:18

Ndipo mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzalandira madalitso kudzera mwa zidzukulu zako, chifukwa iwe wandimvera.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 28:14

Zidzukulu zakozo zidzachuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi. Zidzabalalikira ku mbali zonse: kuzambwe, kuvuma, kumpoto ndi kumwera. Ndipo mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzadalitsidwa kudzera mwa iwe ndi zidzukulu zako.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 30:7

Koma Chauta, Mulungu wanu, adzagwetsa matemberero onse aja pa adani anu amene adakuzunzani.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:9

Koma inu ndinu fuko losankhidwa, ansembe achifumu, mtundu wopatulika, anthu akeake a Mulungu. Adakusankhani kuti mukalalike ntchito zamphamvu za Iye amene adakuitanani kuti mutuluke mu mdima, mukaloŵe m'kuŵala kwake kodabwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 15:4

Palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu a mtundu wanu amene adzasauke, (poti Chauta, Mulungu wanu, adzakudalitsani m'dziko limene Iye adzakupatsani ngati choloŵa chanu,)

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 49:22

Ambuye Chauta akunena kuti, “Ndidzakodola anthu a mitundu ina. Ndidzaŵakwezera mbendera kuti adzabwere. Tsono adzabwera nawo ana ako aamuna ataŵatengera m'manja, ndiponso ana ako aakazi, ataŵasenzera pa mapewa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 132:13-14

Chauta wasankhula Ziyoni, akufuna kuti akhale malo ake okhalamo.

Akuti, “Ameneŵa ndiwo malo anga opumuliramo mpaka muyaya. Ndidzakhala kuno chifukwa ndakufunitsitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 126:1-2

Pamene Chauta adabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati anthu amene akulota.

Pamenepo tidasekera kwambiri, ndipo tidalulutira ndi chimwemwe. Tsono mitundu ina ya anthu inkanena kuti, “Chauta waŵachitira zazikulu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 37:21-22

pamenepo udzaŵauze kuti Ine Ambuye Chauta ndikuti, Ndidzaŵaitana Aisraele kuchokera ku malo ao aukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ndidzaŵasonkhanitsa kuchokera ku mphepo zinai ndi kuŵabwezera ku dziko lao.

Ndidzaŵasandutsa mtundu umodzi m'dzikomo, ku mapiri a Israele, ndipo adzakhala ndi mfumu imodzi yokha. Sadzakhalanso mitundu iŵiri ya anthu kapena kugaŵikana maufumu aŵiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 62:6-7

Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndaikapo alonda, usana wonse ndi usiku wonse sadzakhala chete. Inu amene mumakumbutsa Chauta za malonjezo ake, musapumule.

Musaleke kumkumbutsa mpaka atakhazikitsanso Yerusalemu, ndi kuusandutsa mzinda umene dziko lapansi lidzautamanda.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 27:29

Anthu azikutumikira, mitundu ya anthu izikugwadira. Ukhale wolamulira pakati pa abale ako, zidzukulu za mai wako zizikugwadira. Atembereredwe onse okutemberera, ndipo adalitsidwe onse okudalitsa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 46:4

Koma kuli mtsinje umene mifuleni yake imasangalatsa anthu amumzinda wa Mulungu, malo oyera okhalako Wopambanazonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:5

Ngodala anthu ofatsa, pakuti Mulungu adzaŵapatsa dziko la pansi pano kuti likhale lao.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 36:24-26

Ndidzakutulutsani pakati pa mitundu inayo, ndidzakusonkhanitsani kuchokera ku dziko lililonse, ndipo ndidzakubwezani ku dziko lanu.

Ndidzakuwazani madzi angwiro, ndipo mudzayera, zonse zokuipitsani zidzachoka. Ndiponso ndidzakuyeretsani pochotsa mafano anu onse.

Ndidzakupatsani mtima watsopano ndi kuloŵetsa mzimu watsopano mwa inu. Ndidzakuchotserani mtima wanu wouma ngati mwalawo ndi kukupatsani mtima wofeŵa ngati mnofu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 54:2-3

“Ukuze malo omangapo hema lako, ufunyulule kwambiri nsalu zake. Usalephere, utalikitse zingwe zake, ndipo ulimbitse zikhomo zake.

Udzasendeza malire ake uku ndi uku. Zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina, zidzadzaza mizinda imene idasiyidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 87:1-3

Mzinda umene Chauta adamanga maziko ake, uli pa phiri loyera.

Chauta amakonda mzinda wa Ziyoni amaukonda kupambana kwina kulikonse kumene zidzukulu za Yakobe zimakhala.

Iwe mzinda wa Mulungu, anthu amakamba zambiri zotamanda iwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 12:10

“Tsono anthu a pa banja la Davide ndi anthu onse a ku Yerusalemu ndidzaŵadzaza ndi mtima wachifundo ndi wakupemphera. Motero adzati atamuyang'ana amene adambaya, adzamlira kwabasi monga muja amamlirira mwana akakhala mmodzi yekha. Adzamliradi kwambiri monga muja amamlirira mwana wachisambamu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 34:26-27

Ndidzakhazika anthu anga kufupi ndi phiri langa, ndipo ndidzaŵagwetsera mvula pa nthaŵi yake, mvula yake ya madalitso.

Mitengo ya m'minda idzabereka zipatso, ndipo minda idzakhala ndi zokolola zake, tsono anthu adzakhala mwamtendere m'dziko lao. Adzadziŵa kuti Ine ndine Chauta, pamene ndidzathyole magoli ao ndi kuŵapulumutsa kwa amene adaŵagwira ukapolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 115:14-15

Chauta akudalitseni inu, pamodzi ndi zidzukulu zanu zomwe.

Akudalitseni Chauta, amene adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 49:22-23

Ambuye Chauta akunena kuti, “Ndidzakodola anthu a mitundu ina. Ndidzaŵakwezera mbendera kuti adzabwere. Tsono adzabwera nawo ana ako aamuna ataŵatengera m'manja, ndiponso ana ako aakazi, ataŵasenzera pa mapewa.

Mafumu adzakhala ngati atate okulerani, akazi a mafumuwo adzakhala ngati amai okuyamwitsani. Adzagwetsa nkhope zao pansi ndi kukuŵeramirani. Adzaseteka fumbi la m'mapazi mwanu modzichepetsa. Pamenepo mudzadziŵa kuti Ine ndine Chauta, ndipo amene amakhulupirira Ine sadzachita manyazi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 31:10

“Mverani mau a Chauta, inu anthu a mitundu yonse. Mulalike mauwo ku maiko akutali a m'mbali mwa nyanja. Mulungu amene adabalalitsa Aisraele adzaŵasonkhanitsanso. Adzaŵasamala monga momwe mbusa amasamalira nkhosa zake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:1-2

Mulungu adzambatuke, adani ake amwazikane. Onse amene amamuda, athaŵe pamaso pake.

Anthu anu adapezamo malo okhala. Inu Mulungu, mudapatsa anthu osauka zosoŵa zao mwa ubwino wanu.

Ambuye apereka lamulo. Nchachikulu chiŵerengero cha amene abwera ndi uthenga wakuti,

“Mafumu a magulu a ankhondo akuthaŵa, indedi akuthaŵa. Tsono azimai ku mudzi akugaŵana zofunkha, ngakhale atsalira pakati pa makola ankhosa.

“Zofunkhazo zikuwoneka ngati mapiko a nkhunda okutidwa ndi siliva, nthenga zake nzokutidwa ndi golide wonyezemira.”

Pamene Mphambe adabalalitsa mafumu kumeneko, ku Zalimoni kudagwa chisanu choopsa.

Iwe phiri la Basani, phiri laulemerero, Iwe phiri la Basani, phiri la nsonga zambiri!

Iwe phiri la nsonga zambiriwe, chifukwa chiyani ukuliyang'ana mwansanje phiri limene Mulungu adasankha kuti azikhalapo? Ndithu Chauta adzakhalapo mpaka muyaya.

Ambuye adafika ku malo ao oyera kuchokera ku Sinai, ali ndi magaleta amphamvu zikwi zambirimbiri.

Inu mudakwera kumwamba, mutatenga am'ndende ambiri, ndipo mudalandira mphatso kwa anthu, ngakhale kwa anthu oukira, kuti mudzakhale kumeneko, Inu Chauta Mulungu.

Atamandike Ambuye, Mulungu Mpulumutsi wathu, amene amanyamula katundu wathu tsiku ndi tsiku.

Amwazeni iwowo monga m'mene mphepo imachitira utsi. Anthu oipa aonongeke pamaso pa Mulungu, monga m'mene sera amasungunukira pa moto.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 26:8

Inu Chauta, ndimakonda Nyumba imene mumakhalamo, ndiye kuti malo amene kuli ulemerero wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Malaki 1:11

Dzina langa nlalikulu pakati pa mitundu ya anthu kuchokera kuvuma mpaka kuzambwe. Kulikonse anthu amapereka nsembe zofukiza ndi mphatso zangwiro m'dzina langa. Pajatu dzina langa nlalikulu pakati pa mitundu ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 2:2-3

Pa masiku akudzaŵa phiri la Nyumba ya Chauta adzalisandutsa lalitali koposa mapiri ena onse, lidzangoti joo pamwamba pa magomo onse. Mitundu yonse ya anthu idzathamangira ku phiri limenelo.

Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano asiliva ndi agolide, amene adaadzipangira kuti azipembedza.

Adzathaŵira m'mapanga am'matanthwe ndi m'ming'alu yam'nthaka, kuthaŵa mkwiyo wa Chauta, kuthaŵanso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzabwere kudzaopsa dziko lapansi.

Musakhulupirirenso munthu, poti moyo wake sukhalira kutha. Nanga iye nkumuyesanso kanthu ngati!

Anthu a mitundu yambiri adzabwera, ndipo adzanena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Chauta, ku Nyumba ya Mulungu wa Yakobe. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda m'njira zakezo.” Pakutitu nku Ziyoni kumene kudzafumira malangizo akewo, nku Yerusalemu kumene kudzachokera mau a Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 11:26

Pamenepo Aisraele onse adzapulumuka. Ndi monga Malembo anenera kuti, “Mpulumutsi adzachokera ku Ziyoni, adzachotsera zidzukulu za Yakobe kuipa kwao konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 30:19-20

Tsopano ndikukupatsani mpata woti musankhe, kapena moyo kapena imfa, madalitso a Mulungu kapena matemberero ake. Zonse zakumwamba ndi zapansi zikhale mboni za zimene ndakuuzani lerozi. Tsono sankhani moyo,

Tsono inuyo ndi zidzukulu zanu mudzabwerera kwa Chauta, ndipo mau ake amene ndikukupatsani leroŵa mudzaŵamvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.

mukonde Chauta, Mulungu wanu, muzimvera mau ake ndi kukhala okhulupirika kwa Iye, kuti inu ndi zidzukulu zanu mudzakhalitsemo m'dziko limene adalonjeza kuti adzapatsa makolo anu, Abrahamu, Isaki ndi Yakobe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:4

Ngodala anthu amene amakhala m'Nyumba mwanu, namaimba nyimbo zotamanda Inu nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:34-35

Vomerezani kuti Mulungu ndi wamphamvu, ulamuliro wake uli pa Israele, mphamvu zake zili mu mlengalenga.

Mulungu ndi woopsa m'malo ake opatulika, Mulungu wa Israele ndiye amapatsa mphamvu ndi kuŵalimbikitsa anthu ake. Mulungu atamandike.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Chauta Wamuyaya, Ambuye Wapamwamba! Ndikukutamandani chifukwa ndinu Wolungama, Woyera, ndi woyenera kutamandidwa ndi kupembedzedwa konse. Atate wabwino, m'dzina la Yesu ndikukuthokozani chifukwa ndimapeza chimwemwe chenicheni pa gawo lililonse la moyo wanga chifukwa cha Mzimu Woyera wanu. Ndikupemphani kuti pamene tsiku langa likupita mundithandize kukumbukira chikondi chanu ndi malonjezo anu, chifukwa ndiye gwero la chimwemwe changa chonse. Ambuye Yesu, ndithandizeni kukhala ndi mtima woyamikira nthawi zonse pazinthu zonse, kuti chimwemwe chanu chikhale mwa ine, ngakhale pazinthu zovuta kwambiri, chifukwa ndikudziwa kuti chochitika chilichonse chili ndi cholinga chamtengo wapatali, phunziro losayerekezeka, ndi kuphunzira. Mawu anu amati: "Malemba anu ndi cholowa changa chosatha; ndiwo chimwemwe cha mtima wanga". Ambuye, tsopano munditsogolere mu Ukhala Wanu kuti ndilandire mtendere wanu mpaka udzadzaze mokwanira kuti ndidalitse anthu ozungulira ine. Zikomo Mulungu, chifukwa chondikondera, kundisamalira, kundipatsa zosowa zanga, ndi kuteteza banja langa. Ulemerero wonse ukhale wanu Ambuye. M'dzina la Yesu, Ameni.