Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


108 Mau a Mulungu Okondwera ndi Yehova

108 Mau a Mulungu Okondwera ndi Yehova

M’salmo 37:4 Davide anati, “Sangalala mwa Yehova, ndipo adzakupatsa zokhumba za mtima wako.” Kusangalala kumeneku, ndiko kukhala wachimwemwe chenicheni, wokhutira ndi chinthu chomwe chimatipatsa chimwemwe choona. Baibulo limatiphunzitsa kuti chimwemwe choonachi chimapezeka mwa Mulungu yekha. Tikamasangalala mwa Iye, mavuto athu ndi zovuta zathu zimachepa, podziwa kuti Iye ndiye wolamulira wa miyoyo yathu.

Tikamasangalala mwa Mulungu, ubwenzi wathu ndi Iye umalimba, timamuyandikira kwambiri, ndipo timaphunzira kudalira malonjezo ake. Kusangalala mwa Iye kumatithandizanso kukhala oyamikira, podziwa kuti madalitso athu onse amachokera ku chikondi chake ndi chisamaliro chake pa ife.

Koma kusangalala mwa Mulungu sikutanthauza kunyalanyaza maudindo athu a tsiku ndi tsiku kapena kuthawa mavuto. M’malomwake, kumatanthauza kupeza mphamvu ndi nzeru mwa Iye kuti tithe kuthana ndi mavutowo molimba mtima komanso modalira.

Kumbukira kuti kusangalala mwa Mulungu kumatipatsa moyo wabwino komanso watanthauzo. Kumatithandiza kupeza chikhutiro choona ndi kudziwa cholinga chimene Iye ali nacho pa moyo wathu.

Pakati pa zovuta ndi zosokoneza za dziko lino, tikumbukire kuti mwa Mulungu yekha ndi komwe tingapeze chimwemwe chimene mitima yathu imakhumba.




Masalimo 119:16

Ndidzakondwera ndi malamulo anu, ndipo mau anu sindidzaŵaiŵala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 15:16

Nditamva mau anu, ndidaŵalandira bwino, mauwo adandipatsa chimwemwe ndi chisangalalo. Paja Inu Chauta Wamphamvuzonse, ndimadziŵika ndi dzina lanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 22:8

Amati, “Unkadalira Chauta, Chauta yemweyo akupulumutse. Akulanditsetu tsono, popeza kuti amakukonda.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:4

Muzikondwa mwa Ambuye nthaŵi zonse. Ndikubwerezanso kuti, “Muzikondwa.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 16:11

Mumandiwonetsa njira ya ku moyo. Ndimapeza chimwemwe chachikulu kumene kuli Inu, ndidzasangalala mpaka muyaya ku dzanja lanu lamanja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 61:10

Tsono ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Chauta, mtima wanga ukukondwadi chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso. Wandiveka mkanjo wa chilungamo. Zinali ngati mkwati wamwamuna wavala nkhata ya maluŵa m'khosi, ndiponso ngati mkwati wamkazi wavala mikanda ya mtengo wapatali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:4

Kondwa mwa Chauta, ndipo adzakupatsa zimene mtima wako ukukhumba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 40:8

Ndimakonda kuchita zimene mumafuna, Inu Mulungu wanga, malamulo anu ali mumtima mwanga.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 1:2

koma wokondwerera kumvera malamulo a Chauta, nkumasinkhasinkha za malamulowo usana ndi usiku.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 112:1

Tamandani Chauta! Ngwodala munthu woopa Chauta, wokonda kusunga malamulo ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 2:1

Hana adapemphera nati, “Mtima wanga ukukondwa chifukwa cha zimene Chauta wandichitira, Ndikuyenda ndi mdidi chifukwa cha Chauta. Pakamwa panga pakula nkuseka adani anga monyodola. Ndakondwa kwambiri chifukwa mwandipulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 8:10

Tsono Nehemiya adapitiriza nati, “Kazipitani, mukachite phwando ku nyumba, kenaka muŵapatseko anzanu amene sadakonze kanthu. Pakuti lero ndi tsiku loyera kwa Chauta, Mulungu wathu. Tsono musakhale ndi chisoni, popeza kuti chimwemwe chimene Chauta amakupatsani, chimakulimbikitsani.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 27:4

Ndapempha chinthu chimodzi chokha kwa Chauta, chinthu chofunika kwambiri, chakuti ndizikhala m'Nyumba ya Chauta masiku onse a moyo wanga, kuti ndizikondwera ndi kukoma kwake kwa Chauta ndi kuti ndizipembedza Iye m'Nyumba mwakemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 9:25

Motero adagonjetsa mizinda yamalinga nalanda dziko lachonde, nyumba zodzaza ndi zinthu zabwino, zitsime zokumbakumba, minda yamphesa, minda yaolivi ndiponso mitengo yazipatso yochuluka kwambiri. Choncho iwowo ankadya, namakhuta, mpaka kumanenepa, ndipo ankakondwa chifukwa cha ubwino wanu, Inu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:8

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino. Ngwodala munthu wothaŵira kwa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 58:14

Mukatero ndiye kuti mudzakondwa mwa Ine, Chauta, ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi. Mudzadyerera dziko limene ndidapatsa Yakobe kholo lanu. Ine Chauta ndalankhula zimenezi ndi pakamwa panga.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:35

Munditsogolere kuti ndimvere malamulo anu, chifukwa ndimakondwera nawo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 9:2

Ndidzakondwa ndi kusangalala chifukwa cha Inu, ndidzaimba nyimbo zotamanda dzina lanu, Inu Wopambanazonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 22:26

Ukatero udzakondwa naye Mphambe, Udzaikapo mtima pa Mulungu mwamtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:92

Malamulo anu akadapanda kundisangalatsa, bwenzi nditafa ndi mazunzo anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:19

Pamene nkhaŵa zikundichulukira, Inu mumasangalatsa mtima wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:10

Mphamvu za kavalo saziyesa kanthu, mphamvu za ankhondo sazisamala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:2

Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene saadya? Chifukwa chiyani malipiro anu mukuwonongera zinthu zimene sizingakuchotseni njala? Mvetsetsani zimene ndikunena Ine, ndipo muzidya zimene zili zabwino, muzidzisangalatsa ndi zakudya zonona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 14:10

Chauta akunena za anthu ameneŵa kuti, “Amakonda kuyendayenda kumene afuna, ndipo sangathe kudziletsa. Nchifukwa chake Ine Chauta sindingakondwere nawo, ndipo tsopano ndidzakumbukira kuipa kwao, ndidzaŵalanga chifukwa cha machimo ao.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 8:30-31

Nthaŵiyo nkuti ndili pambalipa ngati mmisiri wake, ndikumkondweretsa tsiku ndi tsiku, ndikusangalala pamaso pake nthaŵi zonse. Ndinkasangalala m'dziko lake lokhalamo anthu, ndi kumakondwa nawo ana a anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 7:18

Kodi ndani ali Mulungu ngati Inu, amene amakhululukira machimo ndi kuiŵala zolakwa za anthu anu otsala? Simusunga mkwiyo mpaka muyaya, chifukwa muli ndi chikondi chosasinthika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:47

Inetu ndimasangalala ndi malamulo anu amene ndimaŵakonda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:111

Malamulo anu ndiye madalitso anga mpaka muyaya, zoonadi, ndiwo amene amasangalatsa mtima wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:13

Mulungu amene amatipatsa chikhulupiriro, adzaze mitima yanu ndi chimwemwe ndi mtendere pakumvera Iye, kuti chiyembekezo chanu chizikulirakulira ndi mphamvu za Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 19:8

Malangizo a Chauta ndi olungama, amasangalatsa mtima. Malamulo a Chauta ndi olungama, amapatsa mtima womvetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:23

Chauta amatsogolera mayendedwe a munthu wolungama, amatchinjiriza amene njira zake zimakomera Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:8

Iyeyu simudamuwone, komabe mumamkonda. Ngakhale simukumuwona tsopano, mumamkhulupirira ndipo mumakondwera ndi chimwemwe chachikulu ndi chosaneneka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:11

“Ndakuuzani zimenezi kuti chimwemwe changa chikhale mwa inu, kuti chimwemwe chanu chikhale chathunthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:114

Inu ndinu malo anga obisalako ndiponso chishango changa, ndimakhulupirira mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 92:4

Inu Chauta, mwandisangalatsa ndi ntchito zanu. Motero ndikufuula ndi chimwemwe chifukwa cha zimene Inu mwachita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 100:2

Tumikirani Chauta mosangalala. Bwerani pamaso pake mukuimba mokondwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 149:4

Paja Chauta amakondwera ndi anthu ake, amaŵalemekeza anthu odzichepetsa poŵagonjetsera adani ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zefaniya 3:17

Chauta, Mulungu wako, ali nawe pamodzi, ngati wankhondo wokuthandiza kugonjetsa adani. Adzasangalala ndi chimwemwe chifukwa cha iwe. Adzakubwezera m'chikondi chake. Adzakondwera nawe poimba nyimbo zachimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:14

Kuyenda m'njira ya malamulo anu kumandikondwetsa, kupambana kukhala ndi chuma chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 32:11

Sangalalani ndi kukondwa inu nonse okonda Mulungu, chifukwa cha zimene Chautayo adakuchitirani. Inu anthu ake onse, fuulani ndi chimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:24

Lero ndiye tsiku limene Chauta adalipanga. Tiyeni tikondwe ndi kusangalala pa tsiku limeneli.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 63:5-6

Mudzandikhutitsa ndi zonona, ndipo ndidzakutamandani ndi mau osangalala. Ndikagona pabedi panga ndimalingalira za Inu, usiku wonse ndimasinkhasinkha za Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 12:2-3

“Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga, ndidzamkhulupirira Iye, ndipo sindidzaopa. Pakuti Chauta ndiye mphamvu zondilimbitsa, ndiye amene ndimamuimbira, ndiye Mpulumutsi wanga.” Mudzakondwera pokatunga madzi m'zitsime za chipulumutso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Habakuku 3:18

komabe kwanga nkukondwerera mwa Chauta, kwanga nkusangalala chifukwa cha Mulungu Mpulumutsi wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:21

Mitima yathu imasangalala mwa Chauta, popeza kuti timadalira dzina lake loyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:162

Ndimakondwa ndi mau anu monga munthu amene wapeza chuma chambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:11

Koma si pokhapo ai, timakondwera mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu, amene atiyanjanitsa ndi Mulungu tsopano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 3:1

Abale anga, potsiriza ndikuti, “Muzikondwa mwa Ambuye.” Kukulemberaninso mau omwewo sikondilemetsa, ndipo mauwo ngokuthandizani kukhala osakayika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 31:7

Ndidzakondwa ndi kusangalala chifukwa ndinu a chikondi chosasinthika. Mwaona masautso anga, mwazindikira mavuto anga kuti ndi aakulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 97:12

Inu ndi anthu a Chauta, kondwerani mwa iye, ndipo mumthokoze potchula dzina lake loyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 16:27

Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi chimwemwe zili m'Nyumba mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 21:6

Zoonadi, mwaisandutsa yodala kopambana mpaka muyaya. Mwaisangalatsa ndi chimwemwe, chifukwa muli nayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 26:8

Inu Chauta, ife timatsata njira ya malamulo anu, ndipo timakhulupirira Inu. Mtima wathu umangolakalaka kukumbukira ndi kulemekeza dzina lanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 42:1

Monga momwe mbaŵala imakhumbira mtsinje wamadzi, ndimo m'mene mtima wanga umakhumbira Inu Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:16-18

Khalani okondwa nthaŵi zonse. Muzipemphera kosalekeza. Muzithokoza Mulungu pa zonse. Paja zimene Mulungu amafuna kuti muzichita mwa Khristu Yesu nzimenezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 35:9

Motero mtima wanga udzakondwa motamanda Chauta, kukondwerera kuti wandipulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 84:10

Kukhala tsiku limodzi m'mabwalo anu nkwabwino kwambiri kupambana kukhala masiku ambiri kwina kulikonse. Nkadakonda kukhala wapakhomo wa Nyumba ya Mulungu wanga kupambana kukhala m'nyumba za anthu oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:20

Komabe musakondwere chifukwa choti mizimu yoipa ikukugonjerani, koma muzikondwera kuti maina anu adalembedwa Kumwamba.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 89:15-16

Ngodala anthu amene mumaŵaphunzitsa kuimba nyimbo zachikondwerero, amene amayenda m'chikondi chanu, Inu Chauta. Iwowo amakondwa masiku onse chifukwa cha Inu, ndipo amatamanda kulungama kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:7

Pamenepo mtendere wochokera kwa Mulungu, umene uli wopitirira nzeru zonse za anthu, udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:24

Malamulo anu amandikondwetsa, ndiwo amene amandilangiza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:34

Mapemphero anga amkomere Chauta, popeza kuti ndimakondwa mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:103

mau anu ndi otsekemera kwambiri ndikaŵalaŵa. Amatsekemera kuposa uchi m'kamwa mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:167

Mzimu wanga umatsata malamulo anu, pakuti ndimaŵakonda ndi mtima wanga wonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:5

kuti ndiwone zokoma za osankhidwa anu, kuti ndigaŵane nawo chisangalalo cha mtundu wanu, kuti ndipeze ulemerero pamodzi ndi anthu anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:12

Muzikhala okondwa chifukwa cha chiyembekezo chanu. Muzipirira pakati pa masautso, ndipo muzipemphera nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:22

Koma zipatso zimene Mzimu Woyera amabweretsa m'moyo wa munthu ndi izi: Chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, kukhulupirika,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 28:7

Chauta ndiye mphamvu zanga, ndiyenso chishango changa chonditeteza. Ndaika mtima wanga wonse pa Iye. Wandithandiza, choncho mtima wanga ukusangalala, ndipo ndimamthokoza ndi nyimbo yanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 16:24

Mpaka tsopano simunapemphe kanthu potchula dzina langa. Pemphani ndipo mudzalandira, kuti chimwemwe chanu chikhale chathunthu.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 107:9

Chauta amapha ludzu la munthu womva ludzu, amamudyetsa zinthu zabwino munthu womva njala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 71:23

Pakamwa panga padzafuula ndi chimwemwe, pamene ndikukuimbirani nyimbo zotamanda. Nawonso mtima wanga umene mwauwombola, udzaimba moyamika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:4

Tikukulemberani zimenezi kuti chimwemwe chathu chikhale chathunthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:143

Mavuto andigwera pamodzi ndi zoŵaŵa zomwe, koma malamulo anu amandisangalatsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:5

Ngwodala munthu amene chithandizo chake chimafumira kwa Mulungu wa Yakobe, munthu amene amakhulupirira Chauta, Mulungu wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 144:15

Ngodala anthu olandira madalitso ameneŵa. Ngodala anthu amene Mulungu wao ndi Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 97:1

Chauta ndiye Mfumu, anthu a pa dziko lapansi akondwere, anthu onse a m'mbali mwa nyanja asangalale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 35:10

Amene Chauta adaŵaombola adzabwerera, ndipo adzafika ku Ziyoni akuimba mosangalala. Kumeneko adzakondwa mpaka muyaya, ndipo adzaona chimwemwe ndi chisangalalo. Chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:70

Anthu otere ndi opulukira, koma ine ndimakondwa ndi malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:13

Mtima wosangalala umaonetsa nkhope yachimwemwe, koma mtima wachisoni umaphwanya moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 65:18-19

Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya, chifukwa cha zimene ndidzalenga. Ndidzalengadi Yerusalemu watsopano wodzaza ndi chimwemwe, ndipo anthu ake adzakhala okondwa. Mwiniwakene ndidzakhala wokondwa kwambiri chifukwa cha Yerusalemu, ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu ake. Kumeneko sikudzamvekanso kulira kapena kudandaula.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 30:11

Mwasandutsa kulira kwanga kuti kukhale kuvina, mwachotsa chisoni changa ndi kundipatsa chisangalalo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:10

Wakuba amangodzera kuba, kupha ndi kuwononga. Koma Ine ndidabwera kuti nkhosazo zikhale ndi moyo, moyo wake wochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:28

Mudandidziŵitsa njira zopita ku moyo, ndipo mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 51:3

Ndidzatonthoza mtima Ziyoni, ndidzaŵatonthoza mtima okhala ku mabwinja ake. Ngakhale dziko lake ndi chipululu, ndidzalisandutsa ngati Edeni. Ngakhale dziko lake ndi thengo, ndidzalisandutsa ngati munda wa Chauta. Kumeneko anthu adzakondwa ndi kusangalala, adzaimba nyimbo zondilemekeza ndi zondithokoza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 36:8

Mumaŵadyetsa zonona m'nyumba mwanu, ndipo mumaŵamwetsa madzi a mu mtsinje wa madalitso anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 1:25

Mosakayika konse ndikudziŵa kuti ndidzakhalapobe. Ndidzapitiriza kukhala nanu nonsenu, kuthandiza kuti chikhulupiriro chanu chizikula, ndipo chikupatseni chimwemwe koposa kale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:20

Munthu wovomera malangizo, zinthu zidzamuyendera bwino, ndi wodala amene amadalira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 126:3

Ndithudi, Chauta watichitira zazikulu, ndipo tasangalala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 43:4

Tsono ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu amene amandipatsa chimwemwe chopambana. Ndipo ndidzakutamandani ndi pangwe, Inu Mulungu, Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:77

Mundichitire chifundo kuti ndikhale ndi moyo, pakuti malamulo anu amandikondwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:174

Ndikulakalaka nthaŵi yoti mudzandipulumutse. Inu Chauta, malamulo anu amandikondwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:11

Koma anthu ofatsa adzalandira dziko kuti likhale lao, ndipo adzakhala pa mtendere wosaneneka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:47

ndipo mzimu wanga ukukondwera mwa Mulungu, Mpulumutsi wanga,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 63:3

Ndidzakutamandani chifukwa chikondi chanu nchabwino kupambana moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 9:3

Inu Chauta, mwauchulukitsa mtundu wanu, mwaonjezera kukondwa kwa anthu anu. Iwo akukondwa pamaso panu monga m'mene anthu amakondwera nthaŵi ya masika, monganso m'mene anthu amakondwera pogaŵana zofunkha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:13

Ngwodala munthu amene wapeza nzeru, amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 90:14

Tidzazeni m'maŵa mulimonse ndi chikondi chanu chosasinthika, kuti tizikondwa ndi kusangalala masiku athu onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 63:7

Inu mwakhala chithandizo changa, motero ndikuimba ndi chimwemwe pansi pa mapiko anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:17

Mu ufumu wa Mulungu chachikulu si chakudya kapena zakumwa ai, koma chilungamo, mtendere ndi chimwemwe, zimene Mzimu Woyera amapereka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:5

Adzaimba nyimbo zotamanda njira za Chauta, pakuti ulemerero wa Chauta ndi waukulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:72

Malamulo a pakamwa panu amandikomera kuposa ndalama zikwizikwi zagolide ndi zasiliva.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 65:4

Ngwodala munthu amene Inu mumamsankha nkubwera naye kudzakhala m'mabwalo anu. Mutikhutitse ndi zinthu zabwino za m'Nyumba yanu, Nyumba yanu yoyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 95:1-2

Bwerani, timuimbire Chauta. Tiyeni tifuule ndi chimwemwe kwa Iye, thanthwe lotipulumutsa. Pa zaka makumi anai ndidaipidwa ndi mbadwo umenewo, choncho ndidati, “Ameneŵa ndi anthu osakhulupirika, sasamalako njira zanga.” Choncho ndidakwiya nkulumbira kuti anthuwo sadzaloŵa ku malo anga ampumulo. Tiyeni, tikafike pamaso pake, tikamthokoze, tiyeni tifuule kwa Iye ndi chimwemwe, timuimbire nyimbo zotamanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:17-18

Ndipotu mwina mwake ndidzaphedwa, magazi anga nkukhala ngati otsiridwa pa nsembe imene chikhulupiriro chanu chikupereka kwa Mulungu. Ngati ndi choncho ndili wokondwa, ndipo ndikusangalala nanu pamodzi nonsenu. Chimodzimodzi inunso muzikondwa, ndi kusangalala nane pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 16:10

Munyadire dzina lake loyera. Ikondwe mitima ya anthu amene amapembedza Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 84:2

Mtima wanga ukulakalaka, mpaka kukomoka, kufunitsitsa kuwona mabwalo a Chauta. Inu Mulungu wamoyo, ndikukuimbirani mwachimwemwe ndi mtima wanga wonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:165

Anthu okonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, palibe china chotha kuŵagwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 43:5

Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika choncho m'kati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamtamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Mulungu wanga, kukhalapo kwanu n'kodabwitsa kwa ine. Mwa inu ndimapeza mtendere, chimwemwe, bata, ndi chikondi chanu chosatha. Muli nazo zonse zomwe ndikusowa; ndinu mphamvu yanga, mlengi wanga. Palibe tsiku limodzi lomwe sindiona chifundo chanu chachikulu pa moyo wanga. Munthirira ine ndi chisomo ndi ubwino wanu, mundidzaza ndi madalitso ochuluka omwe amandipangitsa kusangalala. Sindingathe kukhala wopanda chimwemwe pamaso panu. Ndikulakalaka kukhala nanu nthawi zonse, cholinga changa ndi kusangalala tsiku lililonse ndi chikondi chanu ndi mawu anu, ndi kukhala wofukiza wabwino pamaso panu. Ndikupemphani, musalole chilichonse kundilekanitsa ndi chiyero chanu. Mundibatize ndi chikondi chanu, mundigwire mwamphamvu kufikira nditakhala mmodzi ndi inu. Ndinu chikondi changa, chilungamo changa, ndi chitetezo changa. Ndikukuthokozani chifukwa cha zonse; malingaliro anu ndi abwino kwa ine, ndipo ndikudziwa kuti zonse zimandigwirira ntchito yabwino. Ndimakulambirani ndi kukukwezani, m'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa