Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

55 Mau a Mulungu Pa Madalitso

Mulungu adandidalitsa, anandiuza kuti: “Mubalane, muchuluke, mudzaze dziko lapansi, muligonjetse; mulamulire pa nsomba za m’nyanja, pa mbalame za m’mlengalenga, ndi pa zamoyo zonse zakukwawa pa dziko lapansi.” Genesi 1:28

Pamene Mulungu adalenga munthu ndi kuulula chifuniro chake pa dziko lapansi, adampatsa dalitso lake. Sikofunika kokha kupeza ndi kulandira dalitso la Mulungu m'moyo, komanso momwe timaliliri ndi ntchito ndikofunikira kwambiri. Mu dalitso la Khristu, ndife odala, chifukwa Mulungu anasankha kutidalitsa ndi madalitso onse. Sanatidalitse chifukwa chakuti ndife abwino, kapena chifukwa cha ntchito zathu zabwino, koma chifukwa anatikonda mwa Iye kuyambira chiyambi cha dziko, ndipo anatiitana ndi chiitano choyera. Kuyambira pano, sungani mawu a Mulungu mumtima mwanu, ndipo dalitso lake lidzakutsatirani kulikonse, chifukwa kuyambira kalekale, Atate anasankha kukudalitsani mumtima mwake.


Deuteronomo 15:6

Chauta adzakudalitsani inu monga momwe adalonjezera. Mudzakongoza mitundu yambiri, koma inuyo simudzakongola kwa wina aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri, koma palibe mtundu wina uliwonse umene udzakulamulireni inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 23:25

Muzipembedza Chauta, Mulungu wanu, tsono ndidzakudalitsani pokupatsani chakudya ndi madzi, ndipo ndidzakuchiritsani matenda onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:3

Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu. Mwa Khristu Iye adatipatsa madalitso onse auzimu Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 17:27

Tsono ndikukupemphani kuti mudalitse mokondwa banja la ine mtumiki wanu, likhalebe pamaso panu mpaka muyaya. Pajatu zimene Inu Chauta mwazidalitsa, zimakhala zodalitsidwadi mpaka muyaya.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:22

Madalitso a Chauta ndiwo amalemeretsa, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Numeri 6:24-26

Chauta akudalitseni, ndipo akusungeni.

Chauta akuyang'aneni mwachikondi ndipo akukomereni mtima.

Chauta akuyang'aneni mwachifundo, ndipo akupatseni mtendere.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 115:13

Adzadalitsa amene amamlemekeza, anthu wamba ndi apamwamba omwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 1:1-3

Ngwodala munthu wosatsata uphungu wa anthu oipa, wosatsanzira mayendedwe a anthu ochimwa, wosakhala nawo m'gulu la anthu onyoza Mulungu,

koma wokondwerera kumvera malamulo a Chauta, nkumasinkhasinkha za malamulowo usana ndi usiku.

Munthuyo ali ngati mtengo wobzalidwa m'mbali mwa mtsinje wa madzi, ngati mtengo wobereka zipatso pa nthaŵi yake, umene masamba ake safota konse. Zochita zake zonse zimamuyendera bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 29:11

Zoona, Ine ndiye amene ndimadziŵa zimene ndidakukonzerani, zakuti mudzakhala pabwino osati poipa, kuti mukhale ndi chiyembekezo chenicheni pa zakutsogolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 34:26

Ndidzakhazika anthu anga kufupi ndi phiri langa, ndipo ndidzaŵagwetsera mvula pa nthaŵi yake, mvula yake ya madalitso.

Mutu    |  Mabaibulo
Yoswa 1:8

Uziŵerenga buku lamalamuloli, ndipo usana ndi usiku uzisinkhasinkha zolembedwa m'menemo, kuti uzisunge zonse. Tsono ukamatero, udzapeza bwino ndipo udzapambana.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 28:2

Mverani Chauta, Mulungu wanu, ndipo mudzalandira madalitso onse aŵa:

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:3

Uike ntchito zako m'manja mwa Chauta, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 30:16

Mukamamvera malamulo a Chauta, Mulungu wanu, ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero, mukamamkonda Chauta, Mulungu wanu ndi kutsata mau ake onse, pamenepo mudzakhala pabwino ndipo mudzakhala mtundu wa anthu ochuluka. Chauta, Mulungu wanu, adzakudalitsani m'dziko mukukakhalamolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 17:7-8

“Koma ndi wodala munthu wokhulupirira Chauta, amene amagonera pa Chautayo.

Adzakhala ngati mtengo wobzalidwa m'mphepete mwa mtsinje, umene umatambalitsa mizu yake m'mbali mwa madzi. Suwopa kukamatentha, chifukwa masamba ake safota. Pa chaka chachilala sukuda nkhaŵa, ndipo suleka kubala zipatso.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 20:4

Akupatse zimene mtima wako ukukhumba, akuthandize kuti zonse zimene wakonza zichitikedi.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 26:3-4

“Mukamayenda motsata njira zanga ndi kumamvera malamulo anga onse ndi kuŵatsatadi,

Ndidzaononga akachisi anu opembedzerako mafano ku mapiri ndi kugwetsa maguwa anu ofukizirapo lubani, ndipo ndidzaponya mitembo yanu pa mafano opanda moyo, ndipo ndidzadana nanu.

Ndidzasandutsa mizinda yanu kuti ikhale mabwinja, ndidzasandutsanso malo anu achipembedzo kuti akhale opanda anthu, ndipo sindidzalolanso kumva fungo lokoma la zopereka zanu.

Ndidzaononga dziko lanu kotero kuti adani anu amene adzakhale m'menemo adzadabwa.

Ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina ya anthu ndipo ndidzakupirikitsani, lupanga lili pambuyo. Dziko lanu lidzasanduka chipululu, ndipo mizinda yanu idzasanduka mabwinja.

“Pa nyengo imeneyo nthaka idzakondwerera zaka zoipumitsa nthaŵi yonse pamene m'dzikomo mulibe anthu, inu muli m'dziko la adani anu. Pamenepo nthaka idzapuma ndi kukondwerera zaka zopumazo.

Nthaŵi zonse pamene dzikolo lilibe anthu, nthaka idzapuma, kupuma kwake kumene sidapumepo pa zaka zonse pamene inu munkakhalamo.

Ndipo ngakhale ena amene mudzatsalenu, ndidzaika mtima wa mantha mwa inu pamene muli m'dziko la adani anu. Mtswatswa wa tsamba louluka udzakuthaŵitsani. Mudzathaŵa monga m'mene munthu amathaŵira lupanga, ndipo mudzagwa pansi popanda okuthamangitsani.

Mudzaphunthwitsana monga ngati mukuthaŵa nkhondo, ngakhale palibe amene akukupirikitsani. Ndipo simudzakhala ndi mphamvu zoti mulimbane ndi adani anu.

Mudzatha, kuchita kuti psiti, pakati pa mitundu ya anthu, ndipo dziko la adani anu lidzakudyani.

Ngakhale ena amene mudzatsalenu, nanunso mudzazunzika m'dziko la adani anu chifukwa cha machimo anu, ndipo mudzazunzikanso chifukwa cha machimo a makolo anu.

ndidzakupatsani mvula pa nyengo yake, ndipo nthaka idzakubalirani zokolola zochuluka, ndipo mitengo yam'minda idzakubalirani zipatso.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 10:16

Atatero adayamba kuŵafungata anawo, naŵasanjika manja ndi kuŵadalitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 42:12

Motero Chauta adadalitsa Yobe pa masiku ake otsirizaŵa kupambana poyamba paja. Tsono adakhala ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ng'ombe 2,000, ndi abulu aakazi 1,000.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:20

Munthu wovomera malangizo, zinthu zidzamuyendera bwino, ndi wodala amene amadalira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 67:1-2

Inu Mulungu mutikomere mtima ndi kutidalitsa, mutiwunikire ndi chikondi chanu,

Njira yanu idziŵike pa dziko lonse lapansi, chipulumutso chanu chidziŵike pakati pa mitundu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:19

Mulungu wanga ali ndi chuma chochuluka, ndipo mwa Khristu Yesu adzakupatsani zonse zimene mukusoŵa.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 28:1-2

Mukamamvera mau a Chauta, Mulungu wanu, ndi kutsata mosamala malamulo onse amene ndikukupatsani leroŵa, Chauta, Mulungu wanu, adzakukwezani kopambana mitundu yonse ya pa dziko lapansi.

Tsono anthu onse a pa dziko lonse lapansi adzaona kuti Chauta, Mulungu wanu, wakusankhani inu kuti mukhale anthu akeake, ndipo azidzakuwopani.

Chauta adzakudalitsani pokupatsani ana ambiri, zoŵeta zambiri ndiponso zokolola zambiri. Zonsezi adzakupatsani m'dziko limene Iye adalonjeza kwa makolo anu kuti adzakupatsani.

Pa nyengo yake, adzakutumizirani mvula kuchokera kumene amaisunga mu mlengalenga, ndipo adzadalitsa ntchito zanu zonse, kotero kuti inuyo muzidzakongoza mitundu ina zinthu, koma inuyo osakongola kwa aliyense.

Mulungu wanu adzakusandutsani atsogoleri pakati pa mitundu ya anthu, osati otsata pambuyo. Mukamamvera malamulo ake amene ndikukupatsani lero ndi kuŵatsatadi mosamala, mudzakhala okwera nthaŵi zonse, osati otsika.

Choncho pa mau ndikukuuzani leroŵa, musapatuke kumanja kapena kumanzere, pakutsata milungu ina ndi kumaitumikira.

Komatu mukapanda kumvera bwino mau a Chauta, Mulungu wanu, ndi kutsata malamulo ndi malangizo amene ndikukupatsani lero lino, adzakugwerani matemberero aŵa:

Chauta adzatemberera mizinda yanu ndi minda yanu.

Chauta adzatemberera zokolola zanu ndiponso zokandiramo ufa wanu.

Chauta adzakutembererani pokupatsani ana oŵerengeka, zokolola zochepa, ndiponso ng'ombe ndi zoŵeta zina pang'ono chabe.

Chauta adzatemberera ntchito zanu zonse.

Mverani Chauta, Mulungu wanu, ndipo mudzalandira madalitso onse aŵa:

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 9:11

Adzakulemeretsani pa zonse, kuti mukhale oolowa manja ndithu, kotero kuti ambiri adzathokoza Mulungu chifukwa cha mphatso yanu imene tiŵatengereko.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 3:8

Mumatipulumutsa ndinu, Inu Chauta. Madalitso anu akhale pa anthu anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Malaki 3:10

Aliyense abwere ndi chachikhumi chathunthu ku Nyumba yanga, kuti m'menemo mukhale chakudya chambiri. Ndikutero Ine Chauta Wamphamvuzonse. Mundiyese tsono, ndipo muwone ngati sinditsekula zipata zakumwamba ndi kukugwetserani madalitso ochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 8:9

Mukudziŵa kukoma mtima kwa Ambuye athu Yesu Khristu. Ngakhale anali wolemera, adakhala mmphaŵi chifukwa cha inu, kuti ndi umphaŵi wakewo inu mukhale olemera.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:9

Ngodala anthu odzetsa mtendere, pakuti Mulungu adzaŵatcha ana ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 128:1-2

Ngwodala aliyense woopa Chauta, amene amayenda m'njira zake.

Udzadya zimene manja ako adagwirira ntchito. Udzasangalala, ndipo zinthu zidzakuyendera bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 5:29

Ine ndikufuna kuti aziganiza zimenezo masiku onse. Ndikufuna kuti azindiwopa nthaŵi zonse, ndipo kuti azimvera malamulo anga, kuti zinthu ziŵayendere bwino iwowo ndi zidzukulu zao mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 115:15

Akudalitseni Chauta, amene adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:1-2

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasoŵa kanthu.

Amandigoneka pa busa lamsipu. Amanditsogolera ku madzi odikha kokapumulirako.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 12:2-3

Ndidzakusandutsa kholo la mtundu waukulu, ndipo ndidzakudalitsa ndi kukusandutsa wotchuka, kotero kuti udzakhala ngati dalitso kwa anthu ena.

Farao adalamula anthu ake, ndipo iwowo adatulutsa Abramu ndi mkazi wake m'dzikomo, pamodzi ndi zonse zimene anali nazo.

“Ndidzadalitsa onse okudalitsa iwe, koma ndidzatemberera aliyense wokutemberera. Mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzapeza madalitso kudzera mwa iwe.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 128:1-4

Ngwodala aliyense woopa Chauta, amene amayenda m'njira zake.

Udzadya zimene manja ako adagwirira ntchito. Udzasangalala, ndipo zinthu zidzakuyendera bwino.

Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka, m'kati mwa nyuma yako. Ana ako adzakhala ngati tiziphukira taolivi, kuzungulira tebulo lako.

Zoonadi, ndimo m'mene adzakhalire wodala munthu woopa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 6:11

Choncho Bokosi lachipanganolo lidakhala miyezi itatu m'nyumba ya Obededomu wa ku Gati. Ndipo Chauta adadalitsa Obededomu ndi banja lake lonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 20:11

Paja pa masiku asanu ndi limodzi Chauta adalenga zonse zakumwamba, za pa dziko lapansi, nyanja ndi zinthu zonse zam'menemo, koma pa tsiku lachisanu ndi chiŵiri adapumula. Nchifukwa chake Chauta adadalitsa tsiku la Sabata, nalisandutsa loyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 32:26

Apo munthuyo adati, “Taye ndizipita, chifukwa kulikucha.” Koma Yakobe adayankha kuti, “Sindikulola kuti upite mpaka utandidalitsa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:29

Ndikudziŵa kuti ndikadzabwera kumeneko, ndidzabwera ndi madalitso ochuluka a Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:17

Mphatso iliyonse yabwino ndi yangwiro imachokera Kumwamba, kwa Atate a zounikira zonse zakuthambo. Iwo sasinthika konse, ndipo kuŵala kwao sikutsitirika mpang'ono pomwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 29:11

Chauta amapatsa anthu ake mphamvu. Amaŵadalitsa anthu ndi mtendere. Salmo la Davide. Nyimbo yoimba potsekula Nyumba ya Mulungu

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 27:27-29

Atabwera pafupi kudzampsompsona Isaki adanunkhiza zovala zimene Yakobe adaavala, ndipo pompo adamdalitsa, adati, “Fungo lokoma la mwana wanga lili ngati fungo la zokolola za m'munda umene Chauta adaudalitsa.

Mulungu akugwetsere mvula, ndipo minda yako ikhale yobala bwino. Akupatse zakudya ndi zakumwa zambiri.

Anthu azikutumikira, mitundu ya anthu izikugwadira. Ukhale wolamulira pakati pa abale ako, zidzukulu za mai wako zizikugwadira. Atembereredwe onse okutemberera, ndipo adalitsidwe onse okudalitsa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:11

Pakuti Chauta ndiye dzuŵa ndi chishango, amatichitira chifundo ndi kutipatsa ulemu. Chauta saŵamana zabwino anthu oyenda molungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 3:14

Khristu adachita zimenezi, kuti dalitso limene Mulungu adaalonjeza Abrahamu, lipatsidwe kwa anthu a mitundu yonse kudzera mwa Khristu Yesu, ndipo kuti pakukhulupirira tilandire Mzimu Woyera amene Mulungu adaatilonjeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 41:10

Usachite mantha chifukwa Ine ndili nawe, usataye mtima, poti Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu, ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 73:26

Thupi langa ndi mtima wanga zingafooke chotani, Mulungu ndiye mphamvu za mtima wanga ndiyenso wondigaŵira madalitso mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:6

Ngodala anthu amene akumva njala ndi ludzu lofuna chilungamo, pakuti Mulungu adzakwaniritsa zofuna zao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:5

Inu mumandikonzera chakudya, adani anga akuwona. Mumandilandira bwino podzoza mutu wanga ndi mafuta, mumadzaza chikho changa mpaka kusefukira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 16:11

Mumandiwonetsa njira ya ku moyo. Ndimapeza chimwemwe chachikulu kumene kuli Inu, ndidzasangalala mpaka muyaya ku dzanja lanu lamanja.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 9:8

Mulungu angathe kukupatsani madalitso onse pakulu, kuti nthaŵi zonse mukhale ndi zokukwanirani inuyo, ndipo zinanso zochuluka kuti mukathandize pa ntchito zonse zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:32

Iye sadaumire ngakhale Mwana wakewake, koma adampereka chifukwa cha ife tonse. Atatipatsa Mwana wakeyo, nanga Iye nkulephera kutipatsanso zonse mwaulere?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:8

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino. Ngwodala munthu wothaŵira kwa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:5

Mtima wanu usakangamire pa ndalama, ndipo zimene muli nazo, mukhutire nazo. Paja Mulungu adati, “Sindidzakusiyani kapena kukutayani konse.”

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:24

Paja mukudziŵa kuti Ambuye adzakupatsani mphotho. Mphothoyo ndi madalitso amene adalonjeza kudzapatsa anthu ake. Ambuye amene mukuŵatumikirawo ndi Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:14

Mau anga ndi maganizo anga avomerezeke pamaso panu, Inu Chauta, thanthwe langa ndi mpulumutsi wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 136:1

hokozani Chauta chifukwa ngwabwino, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Chauta wanga Wamuyaya, Ambuye Wamkulukulu! Ndikukutambani chifukwa ndinu Wolungama, Woyera, woyenera kutamandidwa ndi kupembedzedwa. Lero ndaima pamaso panu ndikukuthokozani chifukwa cha mwayi wokhala mwana wanu. Ndikupemphani, kuti mukhale ndi ine nthawi zonse m'moyo wanga ndi m'nyumba mwanga, monga momwe munadalitsira Obedi-edomu ndi banja lake. Zikomo chifukwa chondikomera mwapadera, pobzweretsa machiritso, chakudya ndi chitetezo m'moyo wanga. Mwandikomera mwa kuyika anthu oyenera pa nthawi yoyenera m'njira yanga. Chifukwa mwandipangitsa kukhala wopambana nkhondo zanga zonse, mwandipatsa chigonjetso, chifukwa cha izi ndi zina zambiri, ndikupatsani ulemerero ndi ulemu wonse. M'dzina la Yesu. Ameni!