Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


117 Mau a Mulungu Okhudza Chilungamo

117 Mau a Mulungu Okhudza Chilungamo

Ine ndikufuna kukuuzani za chilungamo, chomwe ndi chofala kwambiri m'Baibulo. Tikamakhala olungama, timakhala moyo wotsatira malamulo ndi ziphunzitso za Mulungu. Ndi kuyenda m'njira yabwino, yopanda chinyengo, komanso yowona m'zonse zomwe timachita.

M'Baibulo muli mavesi ambiri ofotokoza kufunika kwa chilungamo. Mwachitsanzo, mu Miyambo 20:7, amati: "Wolungama amakhala ndi moyo wopanda banga; ana ake adzakhala odala pambuyo pake!" Apa tikumva kuti chilungamo sichingotipindulire tokha, komanso chidzapindulire mibadwo yotsatira.

Kukhala wolungama ndi kumvera malamulo a Mulungu ndikutsata njira zake. Salmo 119:11 imatilimbikitsa kusunga mawu a Mulungu mumtima mwathu kuti tisamuchimwire. Chilungamo chimatithandiza pa zochita zathu za tsiku ndi tsiku, kutsogolera zisankho zathu, ndi makhalidwe athu.

Baibulo limatiphunzitsanso kuti Mulungu amadalitsa anthu olungama. Mu Mateyu 5:6, Yesu anati: "Odala ali iwo akumva njala ndi ludzilo la chilungamo, pakuti adzakhutisidwa." Izi zikutanthauza kuti amene amafuna kukhala moyo wolungama adzadalitsidwa ndipo adzapeza chimwemwe mwa Mulungu.

Komabe, sitiyenera kuiwala kuti sitingathe kukhala olungama ndi mphamvu zathu zokha. Aroma 3:22 imatiuza kuti "Chilungamo cha Mulungu chimapezeka mwa chikhulupiriro mwa Yesu Khristu kwa onse okhulupirira." Sikuti ndi ntchito zathu, koma ndi kudalira nsembe ya Yesu pa mtanda ndikukhala moyo womvera Mulungu.

Chilungamo ndi khalidwe lofunika kwambiri lomwe limatiitana kuti tikhale moyo wotsatira mfundo za Atate wathu wakumwamba. Limatilimbikitsa kuti tichite zinthu mwachilungamo, mwaulemu, komanso mowona mtima nthawi zonse. Tikamakhala moyo wolungama, tidzalandira madalitso ndipo tidzapeza chimwemwe mwa Mulungu.




Miyambo 14:2

Woyenda moongoka mtima aopa Yehova; koma wokhota m'njira yake amnyoza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:137

Inu ndinu wolungama, Yehova, ndipo maweruzo anu ndiwo olunjika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 11:7

Pakuti Yehova ndiye wolungama; akonda zolungama; woongoka mtima adzapenya nkhope yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:3

Kuongoka mtima kwa olungama kuwatsogolera; koma kukhota kwa achiwembu kudzawaononga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 97:11

Kuunika kufesekera wolungama, ndi chikondwerero oongoka mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:6

Odala ali akumva njala ndi ludzu la chilungamo; chifukwa adzakhuta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 125:4

Chitirani chokoma, Yehova, iwo okhala okoma; iwo okhala oongoka mumtima mwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 1:6

Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama; koma mayendedwe a oipa adzatayika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 10:5

Mafanowa akunga mtengo wakanjedza, wosemasema, koma osalankhula; ayenera awanyamule, pakuti sangathe kuyenda. Musawaope; pakuti sangathe kuchita choipa, mulibenso mwa iwo kuchita chabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 23:3

Atsitsimutsa moyo wanga; anditsogolera m'mabande a chilungamo, chifukwa cha dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:7

Tiana, munthu asasokeretse inu; iye wakuchita cholungama ali wolungama, monga Iyeyu ali wolungama:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 26:7

Njira ya wolungama ili njira yoongoka; Inu amene muli woongoka, mukonza njira ya wolungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:33

Koma muyambe mwafuna Ufumu wake ndi chilungamo chake, ndipo zonse zimenezo zidzaonjezedwa kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Habakuku 2:4

Taonani, moyo wake udzikuza, wosaongoka m'kati mwake; koma wolungama adzakhala ndi moyo mwa chikhulupiriro chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 2:13

akusiya mayendedwe olungama, akayende m'njira za mdima;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:22

ndicho chilungamo cha Mulungu chimene chichokera mwa chikhulupiriro cha pa Yesu Khristu kwa onse amene akhulupirira; pakuti palibe kusiyana;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:3

Kuchita chilungamo ndi chiweruzo kupambana ndi nsembe kumkonda Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 15:2

Iye wakuyendayo mokwanira, nachita chilungamo, nanena zoonadi mumtima mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:3

Odala iwo amene asunga chiweruzo, iye amene achita chilungamo nthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 7:2

Watha wachifundo m'dziko, palibe woongoka mwa anthu; onsewo alalira mwazi; yense asaka mbale wake ndi ukonde.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:13

ndipo musapereke ziwalo zanu kuuchimo, zikhale zida za chosalungama; koma mudzipereke inu nokha kwa Mulungu, monga amoyo atatuluka mwa akufa, ndi ziwalo zanu kwa Mulungu zikhale zida za chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 7:10

Chikopa changa chili ndi Mulungu, wopulumutsa oongoka mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 33:15

Iye amene ayenda molungama, nanena molunjika; iye amene anyoza phindu lonyenga, nasansa manja ake kusalandira zokometsera milandu, amene atseka makutu ake kusamva za mwazi, natsinzina maso ake kusayang'ana choipa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 32:11

Sekerani mwa Yehova, ndimo kondwerani inu olungama mtima; ndipo fuulani mokondwera nonsenu oongoka mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:21

Wolondola chilungamo ndi chifundo apeza moyo, ndi chilungamo, ndi ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:37

Tapenya wangwiro, ndipo taona woongoka mtima! Pakuti ku matsiriziro ake a munthuyo kuli mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 49:14

Aikidwa m'manda ngati nkhosa; mbusa wao ndi imfa. Ndipo m'mawa mwake oongoka mtima adzakhala mafumu ao; ndipo maonekedwe ao adzanyekera kumanda, kuti pokhala pake padzasowa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 1:11

odzala nacho chipatso cha chilungamo, chimene chili mwa Yesu Khristu, kuchitira Mulungu ulemerero ndi chiyamiko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 64:10

Wolungama adzakondwera mwa Yehova, nadzakhulupirira Iye; ndipo oongoka mtima onse adzalemekeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 112:4

Kuunika kutulukira oongoka mtima mumdima; Iye ndiye wachisomo, ndi wansoni ndi wolungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:24

amene anasenza machimo athu mwini yekha m'thupi mwake pamtanda, kuti ife, titafa kumachimo, tikakhale ndi moyo kutsata chilungamo; ameneyo mikwingwirima yake munachiritsidwa nayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 2:7

Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni; ndiye chikopa cha oyenda molunjika;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 5:12

Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungamayo; mudzamtchinjiriza nacho chivomerezo ngati chikopa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 2:21

Pakuti oongoka mtima adzakhala m'dziko, angwiro nadzatsalamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:11

Koma iwe, munthu wa Mulungu iwe, thawa izi; nutsate chilungamo, chipembedzo, chikhulupiriro, chikondi, chipiriro, chifatso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:9

Woyenda moongoka amayenda osatekeseka; koma wokhotetsa njira zake adzadziwika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 58:8

Pomwepo kuunika kwako kudzawalitsa monga m'mawa, ndi kuchira kwako kudzaonekera msangamsanga; ndipo chilungamo chako chidzakutsogolera; ulemerero wa Yehova udzakhala wotchinjiriza pambuyo pako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:11

Nyumba ya oipa idzapasuka; koma hema wa oongoka mtima adzakula.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:2

Chuma cha uchimo sichithangata; koma chilungamo chipulumutsa kuimfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:6

Waumphawi woyenda mwangwiro apambana ndi yemwe akhotetsa njira zake, angakhale alemera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:28

Pakuti Yehova akonda chiweruzo, ndipo sataya okondedwa ake. Asungika kosatha, koma adzadula mbumba za oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:5

Pakuti ife mwa Mzimu, kuchokera m'chikhulupiriro, tilindira chiyembekezo cha chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 4:5

Koma kwa iye amene sachita, koma akhulupirira Iye amene ayesa osapembedza ngati olungama, chikhulupiriro chake chiwerengedwa chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:6

Chilungamo cha oongoka mtima chidzawapulumutsa; koma achiwembu adzagwidwa ndi mphulupulu yao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:9

Mnyamata adzayeretsa mayendedwe ake bwanji? Akawasamalira monga mwa mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 32:17

Ndi ntchito ya chilungamo idzakhala mtendere; ndi zotsata chilungamo zidzakhala mtendere, ndi kukhulupirika kunthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:29

Ngati mudziwa kuti ali wolungama, muzindikira kuti aliyensenso wakuchita chilungamo abadwa kuchokera mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:6

Ndipo adzaonetsa chilungamo chako monga kuunika, ndi kuweruza kwako monga usana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:17

Pakuti ngati, ndi kulakwa kwa mmodzi, imfa inachita ufumu mwa mmodziyo; makamaka ndithu amene akulandira kuchuluka kwake kwa chisomo ndi kwa mphatso ya chilungamo, adzachita ufumu m'moyo mwa mmodzi, ndiye Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:10

Odala ali akuzunzidwa chifukwa cha chilungamo: chifukwa uli wao Ufumu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 85:13

Chilungamo chidzamtsogolera; ndipo chidzamkonzera mapazi ake njira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:11

Chilango chilichonse, pakuchitika, sichimveka chokondweretsa, komatu chowawa; koma chitatha, chipereka chipatso cha mtendere, kwa iwo ozoloweretsedwa nacho, ndicho cha chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:6

Chilungamo chitchinjiriza woongoka m'njira; koma udyo ugwetsa wochimwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 61:10

Ndidzakondwa kwambiri mwa Yehova, moyo wanga udzakondwerera mwa Mulungu wanga; pakuti Iye wandiveka ine ndi zovala za chipulumutso, nandifunda chofunda cha chilungamo, monga mkwati avala nduwira, ndi monga mkwatibwi adzikometsa yekha ndi miyala yamtengo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:19

Pakuti monga ndi kusamvera kwa munthu mmodzi ambiri anayesedwa ochimwa, chomwecho ndi kumvera kwa mmodzi ambiri adzayesedwa olungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 3:9

ndi kupezedwa mwa Iye, wosati wakukhala nacho chilungamo changa cha m'lamulo, koma chimene cha mwa chikhulupiriro cha Khristu, chilungamocho chochokera mwa Mulungu ndi chikhulupiriro;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 18:20

Yehova anandibwezera monga mwa chilungamo changa; anandisudzula monga mwa kusisira kwa manja anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:14

Chifukwa chake chilimikani, mutadzimangira m'chuuno mwanu ndi choonadi, mutavalanso chapachifuwa cha chilungamo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:8

Zapang'ono, pokhala chilungamo, ziposa phindu lalikulu lopanda chiweruzo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 61:3

ndikakonzere iwo amene alira maliro mu Ziyoni, ndi kuwapatsa chovala kokometsa m'malo mwa phulusa, mafuta akukondwa m'malo mwa maliro, chovala cha matamando m'malo mwa mzimu wopsinjika; kuti iwo atchedwe mitengo ya chilungamo yakuioka Yehova, kuti Iye alemekezedwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:9

Ngati tivomereza machimo athu, ali wokhulupirika ndi wolungama Iye, kuti atikhululukire machimo athu, ndi kutisambitsa kutichotsera chosalungama chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:7

Ndi chikhulupiriro Nowa, pochenjezedwa ndi Mulungu za zinthu zisanapenyeke, ndi pochita mantha, anamanga chingalawa cha kupulumutsiramo iwo a m'nyumba yake; kumene anatsutsa nako dziko lapansi, nakhala wolowa nyumba wa chilungamo chili monga mwa chikhulupiriro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:5

Chilungamo cha wangwiro chimaongola njira yake; koma woipa adzagwa ndi zoipa zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:18

ndipo pamene munamasulidwa kuuchimo, munakhala akapolo a chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:15

Maso a Yehova ali pa olungama mtima, ndipo makutu ake atchereza kulira kwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 15:6

Ndipo anakhulupirira Yehova, ndipo kunayesedwa kwa iye chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:105

Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga, ndi kuunika kwa panjira panga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:21-22

Yesani zonse; sungani chokomacho, Mupewe maonekedwe onse a choipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 5:21

Ameneyo sanadziwe uchimo anamyesera uchimo m'malo mwathu; kuti ife tikhale chilungamo cha Mulungu mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:18

Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbandakucha, kunkabe kuwala kufikira usana woti mbee.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:17

Pakuti m'menemo chaonetsedwa chilungamo cha Mulungu chakuchokera kuchikhulupiriro kuloza kuchikhulupiriro: monga kwalembedwa, Koma munthu wolungama adzakhala ndi moyo ndi chikhulupiriro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:11

Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga, kuti ndisalakwire Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:34

Chilungamo chikuza mtundu wa anthu; koma tchimo lichititsa fuko manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:10

monga kwalembedwa, Palibe mmodzi wolungama, inde palibe mmodzi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 112:6

Popeza sadzagwedezeka nthawi zonse; wolungama adzakumbukika ku nthawi yosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:12

Pakuti maso a Ambuye ali pa olungama, ndi makutu ake akumva pembedzo lao; koma nkhope ya Ambuye ili pa ochita zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:9

pakuti chipatso cha kuunika tichipeza mu ubwino wonse, ndi chilungamo, ndi choonadi,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:15

kuti mukakhale osalakwa ndi oona, ana a Mulungu opanda chilema pakati pa mbadwo wokhotakhota ndi wopotoka, mwa iwo amene muonekera monga mauniko m'dziko lapansi,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 15:1-2

Yehova, ndani adzagonera m'chihema mwanu? Adzagonera ndani m'phiri lanu lopatulika? Iye wakuyendayo mokwanira, nachita chilungamo, nanena zoonadi mumtima mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 51:1

Mverani Ine, inu amene mutsata chilungamo, inu amene mufuna Yehova; yang'anani kuthanthwe, kumene inu munasemedwamo, ndi kuuna kwa dzenje, kumene inu munakumbidwamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:1

Odala angwiro m'mayendedwe ao, akuyenda m'chilamulo cha Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:20

Okhota mtima anyansa Yehova; koma angwiro m'njira zao amsekeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 5:8

Yehova, munditsogolere m'chilungamo chanu, chifukwa cha akundizondawo; mulungamitse njira yanu pamaso panga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 10:4

Pakuti Khristu ali chimaliziro cha lamulo kulinga kuchilungamo kwa aliyense amene akhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 84:11

Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa; Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero; sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 4:8

chotsalira wandiikira ine korona wa chilungamo, amene Ambuye, woweruza wolungama, adzandipatsa ine tsiku lijalo: ndipo si kwa ine ndekha, komatunso kwa onse amene anakonda maonekedwe ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:142

Chilungamo chanu ndicho chilungamo chosatha; ndi chilamulo chanu ndicho choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:15

Kuchita chiweruzo kukondweretsa wolungama; koma kuwaononga akuchita mphulupulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 2:12

ndi kutiphunzitsa ife kuti, pokana chisapembedzo ndi zilakolako za dziko lapansi, tikhale ndi moyo m'dziko lino odziletsa, ndi olungama, ndi opembedza;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:31

Ndipo adamuyesa iye wachilungamo, ku mibadwomibadwo kunthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 56:1

Atero Yehova, Sungani inu chiweruziro, ndi kuchita chilungamo; pakuti chipulumutso changa chili pafupi kudza, ndi chilungamo changa chili pafupi kuti chivumbulutsidwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:30

Koma kwa Iye muli inu mwa Khristu Yesu, amene anayesedwa kwa ife nzeru ya kwa Mulungu, ndi chilungamo ndi chiyeretso ndi chiombolo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 10:10

pakuti ndi mtima munthu akhulupirira kutengapo chilungamo; ndi m'kamwa avomereza kutengapo chipulumutso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 24:4-5

Woyera m'manja, ndi woona m'mtima, ndiye; iye amene sanakweze moyo wake kutsata zachabe, ndipo salumbira monyenga. Iye adzalandira dalitso kwa Yehova, ndi chilungamo kwa Mulungu wa chipulumutso chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:28

M'khwalala la chilungamo muli moyo; m'njira ya mayendedwe ake mulibe imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:16

Kodi simudziwa kuti kwa iye amene mudzipereka eni nokha kukhala akapolo ake akumvera iye, mukhalatu akapolo ake a yemweyo mulikumvera iye; kapena a uchimo kulinga kuimfa, kapena a umvero kulinga kuchilungamo?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Petro 1:5-7

Ndipo mwa ichi chomwe, pakutengeraponso changu chonse, muonjezerapo ukoma pa chikhulupiriro chanu, ndi paukoma chizindikiritso; ndi pachizindikiritso chodziletsa; ndi pachodziletsa chipiriro; ndi pachipiriro chipembedzo; ndi pachipembedzo chikondi cha pa abale; ndi pachikondi cha pa abale chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 97:2

Pomzinga pali mitambo ndi mdima; chilungamo ndi chiweruzo ndizo zolimbitsa mpando wake wachifumu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:7

Wolungama asamalira mlandu wa osauka; koma woipa alibe nzeru yakuudziwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:40

Taonani, ndinalira malangizo anu; mundipatse moyo mwa chilungamo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 1:10-11

kuti mukayese inu zinthu zosiyana; kuti mukakhale a mtima woona ndi wosalakwa, kufikira tsiku la Khristu; odzala nacho chipatso cha chilungamo, chimene chili mwa Yesu Khristu, kuchitira Mulungu ulemerero ndi chiyamiko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:7

Wolungama woyenda mwangwiro, anake adala pambuyo pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:138

Mboni zanuzo mudazilamulira zili zolungama ndi zokhulupirika ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:21

kuti, monga uchimo unachita ufumu muimfa, chomwechonso chisomo chikachite ufumu mwa chilungamo, kufikira moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye wathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:9

Mwakonda chilungamo, ndi kudana nacho choipa; mwa ichi Mulungu, ndiye Mulungu wanu, wakudzozani ndi mafuta a chikondwerero chenicheni koposa anzanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:25

Monga kavumvulu angopita, momwemo woipa kuli zii; koma olungama ndiwo maziko osatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:15

Pakuti chiweruzo chidzabwera kunka kuchilungamo, ndipo oongoka mtima onse adzachitsata.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 54:14

M'chilungamo iwe udzakhazikitsidwa, udzakhala kutali ndi chipsinjo, pakuti sudzaopa; udzakhala kutali ndi mantha, pakuti sadzafika chifupi ndi iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 6:9

Mibadwo ya Nowa ndi iyi: Nowa anali munthu wolungama ndi wangwiro m'mibadwo yake; Nowa anayendabe ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 3:16

Lemba lililonse adaliuzira Mulungu, ndipo lipindulitsa pa chiphunzitso, chitsutsano, chikonzero, chilangizo cha m'chilungamo:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:5

Iye ndiye wakukonda chilungamo ndi chiweruzo, dziko lapansi ladzala ndi chifundo cha Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 11:4-5

koma ndi chilungamo adzaweruza aumphawi, nadzadzudzulira ofatsa a m'dziko moongoka; ndipo adzamenya dziko lapansi ndi chibonga cha kukamwa kwake, nadzapha oipa ndi mpweya wa milomo yake. Ndipo chilungamo chidzakhala mpango wa m'chuuno mwake, ndi chikhulupiriko chidzakhala mpango wa pa zimpso zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:17

Pakuti ufumu wa Mulungu sukhala chakudya ndi chakumwa, koma chilungamo, ndi mtendere, ndi chimwemwe mwa Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:9

Njira ya oipa inyansa Yehova; koma akonda wolondola chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 89:14

Chilungamo ndi chiweruzo ndiwo maziko a mpando wanu wachifumu; chifundo ndi choonadi zitsogolera pankhope panu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:20

Pakuti ndinena ndi inu, ngati chilungamo chanu sichichuluka choposa cha alembi ndi Afarisi, simudzalowa konse mu Ufumu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Woyenerera Mwanawankhosa wa Mulungu, wapamwamba ndi waulemerero, wamuyaya, woyera, woyenera ulemerero ndi kutamandidwa konse. Yesu wanga, moyo wanga wonse, ndidalitsa dzina lanu ndi kulambira ukulu wanu, chifukwa ndinu wolungama, njira yanu ndi yolungama ndipo mulibe choipa chilichonse mwa inu. Ndinu kuunika komwe kumathetsa mdima wanga ndi kunditsogolera mu choonadi chanu. Ambuye wanga, ndikufuna kuti munditsogolere mapazi anga panjira yolungama, mundilole kukhala tsiku lililonse m'kumvera malamulo anu ndi mogwirizana ndi ziphunzitso zanu. Ndithandizeni kupirira mayesero ndi kusapatuka panjira ya choonadi. Moyo wanga ukhale chiwonetsero cha chikondi chanu ndi chifundo chanu, ndipo ndikhale chitsanzo cha umphumphu ndi chilungamo kwa iwo amene ali pafupi nane. Ndi thandizo lanu, nditha kukumana ndi mavuto a tsiku ndi tsiku ndi kugonjetsa mavuto ndi mphamvu ndi kudzichepetsa. Mundipatse nzeru zopangira zisankho zolondola ndi mphamvu zokhazikika m'malamulo ndi malangizo anu. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa