Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 1:6 - Buku Lopatulika

6 Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama; koma mayendedwe a oipa adzatayika.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama; koma mayendedwe a oipa adzatayika.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Paja Chauta amaŵasamalira anthu ake, koma anthu ochimwa adzaonongeka.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 1:6
17 Mawu Ofanana  

Koma adziwa njira ndilowayi; atandiyesa ndidzatuluka ngati golide.


Woipa adzaziona, nadzapsa mtima; adzakukuta mano, nadzasungunuka; chokhumba oipa chidzatayika.


Pamene mzimu wanga unakomoka m'kati mwanga, munadziwa njira yanga. M'njira ndiyendamo ananditchera msampha.


Penyani kudzanja lamanja ndipo muone; palibe wondidziwa; pothawirapo pandisowa; palibe mmodzi wosamalira moyo wanga.


Yehova asunga alendo; agwiriziza mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye; koma akhotetsa njira ya oipa.


Adaniwo atha psiti, apululuka nthawi zonse; ndipo mizindayo mwaipasula, chikumbukiro chao pamodzi chatha.


Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka; koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.


Njira ya oipa inyansa Yehova; koma akonda wolondola chilungamo.


Yehova ali wabwino, ndiye polimbikirapo tsiku la msauko; ndipo adziwa iwo omkhulupirira Iye.


Lowani pa chipata chopapatiza; chifukwa chipata chili chachikulu, ndi njira yakumuka nayo kukuonongeka ili yotakata; ndipo ali ambiri amene alowa pa icho.


Ine ndiye Mbusa Wabwino; ndipo ndizindikira zanga, ndi zanga zindizindikira Ine,


Nkhosa zanga zimva mau anga, ndipo Ine ndizizindikira, ndipo zinditsata Ine.


Koma ndithu maziko a Mulungu aimika pokhazikika, ndi kukhala nacho chizindikiro ichi, Ambuye azindikira iwo amene ali ake; ndipo, Adzipatule kwa chosalungama yense wakutchula dzina la Ambuye.


Koma awo, ngati zamoyo zopanda nzeru, nyama zobadwa kuti zikodwe ndi kuonongedwa, akuchitira mwano pa zinthu osazidziwa, adzaonongeka m'kuononga kwao,


Adzasunga mapazi a okondedwa ake, koma oipawo adzawakhalitsa chete mumdima; pakuti palibe munthu adzapambana ndi mphamvu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa