Kondwerani ndi masiku anu a unyamata, muzitsatira zomwe Mulungu wakukonzerani. Gwiritsani ntchito mphamvu zomwe muli nazo tsopano. Musamadziganizire zochepa chifukwa cha unyamata wanu. Nthawi zina mukadali aang'ono mukhoza kutaya mtima mukaganizira zam'tsogolo, ndipo mwina mungamve kupsinjika maganizo. Koma dziwani kuti Mulungu, Mlengi wanu, ali ndi inu ndipo amayang'anira moyo wanu. Muzimufunafuna ndi mtima wonse, ndipo muziyeretsa tsiku ndi tsiku mwa Iye.
Khalani chitsanzo chabwino kulikonse kumene mungapite, m'chikondi, m'mawu, m'khalidwe, m'chikhulupiriro, ndi m'kuyera. Mulungu amanena m'Mawu ake kuti wachinyamata adzayeretsa njira yake ndi mawu ake. Fufuzani Mawu ake tsiku ndi tsiku ndipo mudzakhala ndi chipambano m'moyo wanu.
Gwiritsani ntchito nthawi iliyonse kukhala pafupi ndi Atate wanu wakumwamba, masiku asanafike pamene simudzakhalanso ndi chimwemwe, kapena mphamvu zomwe muli nazo lero, kapena nthawi yomwe muli nayo lero. Ndinu ofunika kwa Mulungu, Iye ali ndi dongosolo labwino pa moyo wanu ndipo akufuna kulikwaniritsa mwa inu. Mukamamufunafuna Iye, adzakuyikani dongosolo lake mwa inu. (1 Timoteo 4:12) Munthu asanyoze unyamata wanu, koma khalani chitsanzo kwa okhulupirira m'mawu, m'khalidwe, m'chikondi, m'mzimu, m'chikhulupiriro, ndi m'kuyera.
Musakakwatirane nawo, ndiye kuti musakalole ana anu kukwatirana nawo,
kuti angadzaŵasokeretse kuŵachotsa kwa Chauta, Mulungu wanu, namakapembedza nawo milungu ina. Mukadzatero, Chauta adzakukwiyirani, ndipo adzakuwonongani mwamsanga.
Adzasamala maonekedwe ake okha a chipembedzo, nkumakana mphamvu zake. Anthu otere uziŵalewa.
Chauta, Mulungu wa Israele, akunena kuti, “Ndimadana ndi kusudzulana. Ndimadana ndi munthu wochita zankhalwe zotere kwa mkazi wake. Choncho chenjerani, musakhale osakhulupirika. Ndikutero Ine Chauta Wamphamvuzonse.”
Musamagwirizana ndi anthu akunja, monga ngati kuti iwo ndi inu mumafanana. Nanga kulungama kungagwirizane bwanji ndi kusalungama? Kapena kuŵala kungayanjane bwanji ndi mdima?
Wokondedwa, usamatsanzire zoipa, koma zabwino. Aliyense wochita zabwino, ndi mwana wa Mulungu, koma wochita zoipa, sadaone Mulungu.
Inu anthu osakhulupirikanu, kodi simudziŵa kuti kuchita chibwenzi ndi zapansipano nkudana ndi Mulungu? Choncho munthu wofuna kukhala bwenzi la zapansipano, ameneyo amadzisandutsa mdani wa Mulungu.
Musamagwirizana ndi anthu akunja, monga ngati kuti iwo ndi inu mumafanana. Nanga kulungama kungagwirizane bwanji ndi kusalungama? Kapena kuŵala kungayanjane bwanji ndi mdima?
Kodi Khristu nkuvomerezana ndi Satana? Kodi mkhristu ndi mkunja angagaŵanenso chiyani pamodzi?
Musamalikonde dziko lapansi kapena zinthu zapansipano. Munthu akamakonda dziko lapansi, chikondi chokonda Atate sichikhalamo mwa iye.
Kwa anthu am'banja lamulo langa, limenetu kwenikweni ndi lochokera kwa Ambuye, ndi ili: Mkazi asalekane ndi mwamuna wake.
Koma ngati amuleka, akhale wosakwatiwanso, kapena ayanjane nayenso mwamuna wakeyo. Chimodzimodzinso mwamuna asasudzule mkazi wake.
Kwa ena mau anga, osati a Ambuye ai, ndi aŵa: Ngati mkhristu ali ndi mkazi wachikunja, ndipo mkaziyo avomera kukhala naye, mwamunayo asathetse ukwatiwo.
Momwemonso ngati mkhristu wamkazi ali ndi mwamuna wachikunja, ndipo mwamunayo avomera kukhala naye, mkaziyo asathetse ukwatiwo.
Pakuti mwamuna wachikunja uja amadalitsidwa chifukwa cha mkazi wakeyo. Nayenso mkazi wachikunja uja amadalitsidwa chifukwa cha mwamuna wakeyo. Pakadapanda apo, bwenzi ana anu atakhala akunja, koma monga zilirimu, ndi ana a Mulungu.
Koma ngati wakunja uja afuna kuleka mkhristu, amuleke. Zikatero, ndiye kuti mkhristu wamwamunayo kapena wamkaziyo ali ndi ufulu. Mulungu adakuitanani kuti mukhale ndi moyo wamtendere.
Kodi iwe, mkazi wachikhristu, ungadziŵe bwanji ngati udzampulumutsa mwamuna wako? Kapenanso iwe, mwamuna wachikhristu, ungadziŵe bwanji ngati udzapulumutsa mkazi wako?
Mukabwerera m'mbuyo ndi kuphatikizana ndi mitundu yotsalira ili pakati panuyi, ndi kumakwatirana nayo,
pamenepo mudziŵe kuti Chauta, Mulungu wanu, sadzapirikitsa mitundu imeneyi pamaso panu. Koma anthuwo adzakhala ngati msampha kwa inu, kapenanso ngati khwekhwe. Adzakhalanso ngati chikoti choŵaŵa pamsana panu, kapena ngati minga zokulasani m'maso mwanu. Zimenezi zidzachitikabe mpaka inuyo mutatha m'dziko labwinoli limene Chauta, Mulungu wanu, wakupatsani.
Akazi ameneŵa anali a mitundu ija imene Chauta adaauza Aisraele kuti, “Musadzakwatire akazi a mitundu imeneyi, ndipo amuna amitunduyo asadzakwatire akazi a mtundu wanu, poti ndithudi iwowo adzatembenuza mitima yanu, kuti muzitsata milungu yao.” Koma Solomoni ankakondabe akazi a mitundu imeneyo.
Senzani goli langa ndipo phunzirani kwa Ine, pakuti ndine wofatsa ndi wa mtima wodzichepetsa; mukatero mudzapeza mpumulo m'mitima mwanu.
“Kodi Inu ndinu uja ankati adzabwerayu, kapena tiziyembekezera wina?”
Pajatu goli limene ndimakoleka Ine nlosavuta, ndipo katundu amene ndimasenzetsa Ine ngwopepuka.”
Khristu adatimasula kuti tikhale mfulu ndithu. Muzichilimikira tsono, osalola kumangidwanso m'goli la ukapolo.
Nchifukwa chake musakwatitse ana anu aakazi kwa ana ao aamuna, ndipo ana ao aakazi asakwatiwe ndi ana anu aamuna. Musakhale nawo mumtendere kapena kugwirizana nawo pa malonda, ngati mufuna kukhala amphamvu ndi kumadya zabwino za m'dzikomo, ndi kusiyira ana anu dziko limeneli kuti likhale choloŵa chao mpaka muyaya.’
Mkazi amamangika ndi lamulo la ukwati, nthaŵi yonse pamene mwamuna wake ali moyo. Koma mwamuna wake akamwalira, ali ndi ufulu kukwatiwa ndi mwamuna amene iye afuna, malinga ukwatiwo ukhale wachikhristu.
Akazi ameneŵa anali a mitundu ija imene Chauta adaauza Aisraele kuti, “Musadzakwatire akazi a mitundu imeneyi, ndipo amuna amitunduyo asadzakwatire akazi a mtundu wanu, poti ndithudi iwowo adzatembenuza mitima yanu, kuti muzitsata milungu yao.” Koma Solomoni ankakondabe akazi a mitundu imeneyo.
Tsono mkazi wa Hadadiyo adabala mwana wamwamuna dzina lake Genubati, ndipo Tapenesi adalerera Genubati ku nyumba yaufumu. Genubatiyo ankakhala m'nyumba ya Farao pamodzi ndi ana a Farao.
Koma Hadadi atamva ku Ejipitoko kuti Davide adamwalira, ndiponso kuti Yowabu mtsogoleri wankhondo nayenso adafa, adauza Farao kuti, “Loleni ndichoke kuti ndipite ku dziko lakwathu.”
Koma Farao adati, “Chakusoŵa nchiyani kwathu kuno kuti uziti ukufuna kupita ku dziko lakwanu?” Hadadi adauza Farao kuti, “Iyai sizimenezo, mungondilola basi kuti ndizipita.”
Mulungu adautsiranso Solomoni mdani wina, dzina lake Rezoni, mwana wa Eliyada, amene anali atathaŵa kwa mbuyake Hadadezere, mfumu ya ku Zoba.
Munthu ameneyu adasonkhanitsa anthu, nakhala mtsogoleri wao wa gulu la achifwamba. Izi zidachitika pamene Davide adati atagonjetsa Hadadezere, adapha ankhondo a ku Zoba. Tsono Rezoni ndi gulu lake adapita ku Damasiko, nakakhala kumeneko, ndipo anthuwo adamlonga ufumu womalamulira dziko la Siriya.
Rezoni anali mdani wa Israele masiku onse a Solomoni, namamvuta Solomoniyo monga momwe Hadadi ankachitira.
Winanso woukira Solomoni anali Yerobowamu, mwana wa Nebati wa fuko la Efuremu, wa ku Zereda. Anali mmodzi mwa nduna za Solomoni, amene mai wake anali Zeruya, mkazi wamasiye.
Nkhani ya kuukira kwakeyo idaayenda motere: Solomoni adaamanga linga la Milo, nakonza khoma logumuka la mzinda wa Davide bambo wake.
Yerobowamu anali munthu wolimba mtima, ndipo Solomoni ataona kuti mnyamatayo ngwachangu, adamuika kuti akhale kapitao woyang'anira ntchito yathangata m'dziko la ana a Yosefe.
Ndiye tsiku lina pamene Yerobowamu anali pa ulendo kuchokera ku Yerusalemu, mneneri Ahiya wa ku Silo adampeza pa mseu. Ahiyayo anali atavala mwinjiro watsopano, ndipo aŵiriwo anali okha kuthengoko.
Iyeyo adakwatira ana achifumu 700 ndipo anali ndi azikazi 300. Ndipo akaziwo adamsokoneza.
Woyenda ndi anthu anzeru nayenso amakhala ndi nzeru, koma woyenda ndi zitsiru adzaonongeka.
Mfumu Solomoni ankakonda akazi ambiri achilendo. Kuwonjezera pa mwana wamkazi wa Farao, adakwatiranso akazi a mitundu iyi: Amowabu, Aamoni, Aedomu, Asidoni ndi Ahiti.
Nthaŵi imeneyo ndidaona Ayuda amene adaakwatira akazi a ku Asidodi, a ku Amoni ndiponso a ku Mowabu.
Mwakuti theka limodzi la ana ao ankalankhula chilankhulo cha ku Asidodi, sankathanso kulankhula Chiyuda, koma ankalankhula chilankhulo cha anthu a mitundu inayo.
Tsono ndidakangana nawo ndi kuŵatemberera. Ndidamenya ena mwa iwo ndi kuŵazula tsitsi. Ndipo ndidaŵalumbiritsa m'dzina la Mulungu kuti, “Musadzakwatitse ana anu aakazi kwa amuna achilendo, ndipo ana anu aamuna ndi inu nomwe musakwatire akazi achilendo.
Kodi Solomoni mfumu ya Aisraele suja adachimwa chifukwa cha akazi otereŵa? Pakati pa mitundu ya pansi pano panalibe mfumu yofanafana naye. Mulungu ankamkonda ndipo adamuika kuti akhale mfumu ya Aisraele onse. Komabe akazi achilendo adachimwitsa ngakhale iyeyo.
Monga tsopano tizimva kuti inunso mumachita choipa chachikulu chomwechi cha kuipira Mulungu pomakwatira akazi achilendo?”
Usachite naye chibwenzi munthu wopsa mtima msanga, ndipo usamayenda naye munthu waukali,
kuwopa kuti ungadzaphunzireko mayendedwe ake, ndi kukodwa mu msampha.
Ndikukupemphani abale, chenjera nawoni anthu amene amapatutsa anzao naŵachimwitsa. Iwo amaphunzitsa zosiyana ndi zimene inu mudaphunzira. Muziŵalewa,
“Munthu sangathe kutumikira mabwana aŵiri, pakuti kapena adzadana ndi mmodzi nkukonda winayo, kapena adzadzipereka kwa mmodzi nkumanyoza winayo. Simungathe kutumikira onse aŵiri, Mulungu ndi chuma.
Ngwodala munthu wosatsata uphungu wa anthu oipa, wosatsanzira mayendedwe a anthu ochimwa, wosakhala nawo m'gulu la anthu onyoza Mulungu,
koma wokondwerera kumvera malamulo a Chauta, nkumasinkhasinkha za malamulowo usana ndi usiku.
Mukadakhala a mkhalidwe wao, akadakukondani chifukwa cha kukhala anzao. Koma amadana nanu, chifukwa Ine ndidakusankhani pakati pa iwo, motero sindinu anzao.
“Bwerani kwa Ine, inu nonse otopa ndi olemedwa, ndipo Ine ndidzakupatsani mpumulo.
Senzani goli langa ndipo phunzirani kwa Ine, pakuti ndine wofatsa ndi wa mtima wodzichepetsa; mukatero mudzapeza mpumulo m'mitima mwanu.
“Kodi Inu ndinu uja ankati adzabwerayu, kapena tiziyembekezera wina?”
Pajatu goli limene ndimakoleka Ine nlosavuta, ndipo katundu amene ndimasenzetsa Ine ngwopepuka.”
Musamatsanzira makhalidwe a anthu odalira zapansipano, koma Mulungu asinthe moyo wanu wonse pakukupatsani mitima yatsopano. Pamenepo mudzatha kudziŵa zimene Mulungu afuna, ndipo mudzazindikira zimene zili zabwino, zangwiro ndi zomkondwetsa.
Mulungu adaukitsa Ambuye kwa akufa, ndipo mwa mphamvu yake adzatiwukitsa ifenso.
Kodi inu simudziŵa kuti matupi anu ndi ziwalo za Khristu? Monga tsono ine nkutenga ziwalo za Khristu nkuzisandutsa ziwalo za mkazi wadama? Chosatheka!
Kaya simudziŵa kuti munthu amene amadzipereka kwa mkazi wadama, iyeyo ndi mkaziyo amasanduka thupi limodzi? Paja Malembo akuti, “Aŵiriwo adzasanduka thupi limodzi.”
Khalani odziletsa, khalani maso. Mdani wanu Satana amakhala akuyenda uku ndi uku ngati mkango wobangula, kufunafuna woti amudye.
Pambuyo pake ndidamva mau ena ochokera Kumwamba. Adati, “Inu anthu anga, tulukanimo mumzindamo, kuti mungachimwire nawo pamodzi, miliri yao ingakugwereniko.
Nchifukwa chake Ambuye akuti, “Tulukani pakati pao, ndi kudzipatula. Musakhudze kanthu kosayera, ndipo ndidzakulandirani.
Nchifukwa chake musamagwirizane nawo anthu otere.
Inunso kale mudaali mu mdima, koma tsopano muli m'kuŵala, popeza kuti ndinu ao a Ambuye. Tsono muziyenda ngati anthu okhala m'kuŵala.
Usafulumire kumsanjika manja munthu, ndipo usavomerezane ndi anthu ena pa uchimo wao. Iwe usunge bwino kuyera mtima kwako.
Uthaŵe zilakolako zoipa zachinyamata. Pamodzi ndi anthu onse otama Ambuye mopemba ndi mtima woyera, uzifunafuna chilungamo, chikhulupiriro, chikondi ndi mtendere.
Muzikhala ngati ana omvera, osatsatanso zimene munkalakalaka pamene munali osadziŵa.
Koma monga Iye amene adakuitanani ali woyera mtima, inunso khalani oyera mtima m'makhalidwe anu onse.
Paja mau a Mulungu akuti, “Muzikhala oyera mtima popeza kuti Ineyo ndine woyera mtima.”
Musamalikonde dziko lapansi kapena zinthu zapansipano. Munthu akamakonda dziko lapansi, chikondi chokonda Atate sichikhalamo mwa iye.
Paja zonse zapansipano, zilakolako zathupi, zinthu zimene maso amakhumbira, ndiponso kunyadira za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku mkhalidwe woipa wa dziko lapansi.
Ndipotu dziko lapansi likupita, pamodzi ndi zake zonse zimene anthu amazilakalaka. Koma munthu wochita zimene Mulungu afuna, amakhalapo mpaka muyaya.