Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -


143 Mauthenga a Mtendere wa Pabanja

143 Mauthenga a Mtendere wa Pabanja


Yohane 14:27

Mtendere ndikusiyirani inu, mtendere wanga ndikupatsani; Ine sindikupatsani inu monga dziko lapansi lipatsa. Mtima wanu usavutike, kapena usachite mantha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:7

Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana chidziwitso chonse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 29:11

Yehova adzapatsa anthu ake mphamvu, Yehova adzadalitsa anthu ake ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:15

Ndipo mtendere wa Khristu uchite ufumu m'mitima yanu, kulingakonso munaitanidwa m'thupi limodzi; ndipo khalani akuyamika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:13

Ndipo Mulungu wa chiyembekezo adzaze inu ndi chimwemwe chonse ndi mtendere m'kukhulupirira, kuti mukachuluke ndi chiyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 26:3

Inu mudzasunga mtima wokhazikika mu mtendere weniweni, chifukwa ukukhulupirirani Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 4:8

Ndi mtendere ndidzagona pansi, pomwepo ndidzagona tulo; chifukwa Inu, Yehova, mundikhalitsa ine, ndikhale bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:165

Akukonda chilamulo chanu ali nao mtendere wambiri; ndipo alibe chokhumudwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:9

Odala ali akuchita mtendere; chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:1

Nyenyeswa youma, pokhala mtendere, iposa nyumba yodzala nyama yansembe, pali makangano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:11

Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi; nadzakondwera nao mtendere wochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 32:17

Ndi ntchito ya chilungamo idzakhala mtendere; ndi zotsata chilungamo zidzakhala mtendere, ndi kukhulupirika kunthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 85:8

Ndidzamva cholankhula Mulungu Yehova; pakuti adzalankhula zamtendere ndi anthu ake, ndi okondedwa ake; koma asabwererenso kuchita zopusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 3:16

Ndipo Ambuye wa mtendere yekha atipatse ife mtendere nthawi zonse, monsemo. Ambuye akhale ndi inu nonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:14

Londolani mtendere ndi anthu onse, ndi chiyeretso chimene, akapanda ichi, palibe mmodzi adzaona Ambuye:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:14

Futuka pazoipa, nuchite zabwino, funa mtendere ndi kuulondola.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:14

Pakuti Iye ndiye mtendere wathu, amene anachita kuti onse awiri akhale mmodzi, nagumula khoma lakudulitsa pakati,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 46:1-3

Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu m'masautso. Khalani chete, ndipo dziwani kuti Ine ndine Mulungu, Ndidzabuka mwa amitundu, ndidzabuka padziko lapansi. Yehova wa makamu ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu. Chifukwa chake sitidzachita mantha, lingakhale lisandulika dziko lapansi, angakhale mapiri asunthika, nakhala m'kati mwa nyanja. Chinkana madzi ake akokoma, nachita thovu, nagwedezeka mapiri ndi kudzala kwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 54:10

Pakuti mapiri adzachoka, ndi zitunda zidzasunthika; koma kukoma mtima kwanga sikudzakuchokera iwe, kapena kusunthika chipangano changa cha mtendere, ati Yehova amene wakuchitira iwe chifundo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako; umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:114

Inu ndinu pobisalapo panga, ndi chikopa changa; ndiyembekezera mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:18

Ngati nkutheka, monga momwe mukhoza, khalani ndi mtendere ndi anthu onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:22-23

Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro, chifatso, chiletso; pokana zimenezi palibe lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 30:15

Pakuti atero Ambuye, Yehova Woyera wa Israele, M'kubwera ndi m'kupuma inu mudzapulumutsidwa; m'kukhala chete ndi m'kukhulupirira mudzakhala mphamvu yanu; ndipo simunafune.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:6-7

Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi chiyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu. Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana chidziwitso chonse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 11:28-30

Idzani kuno kwa Ine nonsenu akulema ndi kuthodwa, ndipo Ine ndidzakupumulitsani inu. Senzani goli langa, ndipo phunzirani kwa Ine; chifukwa ndili wofatsa ndi wodzichepetsa mtima: ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. nati kwa Iye, Inu ndinu wakudza kodi, kapena tiyembekezere wina? Pakuti goli langa lili lofewa, ndi katundu wanga ali wopepuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 26:12

Phazi langa liponda pachidikha, m'misonkhano ndidzalemekeza Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 127:1

Akapanda kumanga nyumba Yehova, akuimanga agwiritsa ntchito chabe; akapanda kusunga mzinda Yehova, mlonda adikira chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:3

ndi kusamalitsa kusunga umodzi wa Mzimu mwa chimangiriro cha mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:20

mwa Iyenso kuyanjanitsa zinthu zonse kwa Iye mwini, atachita mtendere mwa mwazi wa mtanda wake; mwa Iyetu, kapena za padziko, kapena za mu Mwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:11

ndipo apatuke pachoipa, nachite chabwino; afunefune mtendere ndi kuulondola.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:78

Odzikuza achite manyazi, popeza anandichitira monyenga ndi bodza: Koma ine ndidzalingalira malangizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 128:1-4

Wodala yense wakuopa Yehova, wakuyenda m'njira zake. Pakuti udzadya za ntchito ya manja ako; wodala iwe, ndipo kudzakukomera. Mkazi wako adzanga mpesa wopatsa m'mbali za nyumba yako; ana ako adzanga timitengo ta azitona pozinga podyera pako. Taonani, m'mwemo adzadalitsika munthu wakuopa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 9:6

Pakuti kwa ife mwana wakhanda wabadwa, kwa ife mwana wamwamuna wapatsidwa; ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake, ndipo adzamutcha dzina lake Wodabwitsa, Wauphungu, Mulungu wamphamvu, Atate Wosatha, Kalonga wa mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:6

pakuti chisamaliro cha thupi chili imfa; koma chisamaliro cha mzimu chili moyo ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:14

Ndinakondwera m'njira ya mboni zanu, koposa ndi chuma chonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:18

Mulibe mantha m'chikondi; koma chikondi changwiro chitaya kunja mantha, popeza mantha ali nacho chilango, ndipo wamanthayo sakhala wangwiro m'chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 7:14

ndipo anthu anga otchedwa dzina langa akadzichepetsa, nakapemphera, nakafuna nkhope yanga, nakatembenuka kuleka njira zao zoipa; pamenepo ndidzamvera mu Mwamba, ndi kukhululukira choipa chao, ndi kuchiritsa dziko lao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:17

Kudya masamba, pali chikondano, kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:72

Chilamulo cha pakamwa panu chindikomera koposa golide ndi siliva zikwizikwi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 31:20

Pobisalira pamaso panu mudzawabisa kwa chiwembu cha munthu, mudzawabisa iwo mumsasa kuti muwalanditse pa kutetana kwa malilime.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:33

Koma muyambe mwafuna Ufumu wake ndi chilungamo chake, ndipo zonse zimenezo zidzaonjezedwa kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 122:6-7

Mupempherere mtendere wa Yerusalemu; akukonda inu adzaona phindu. M'linga mwako mukhale mtendere, m'nyumba za mafumu mukhale phindu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 43:2

Pamene udulitsa pamadzi ndili pamodzi ndi iwe; ndi pooloka mitsinje sidzakukokolola; pakupyola pamoto sudzapsa; ngakhale lawi silidzakutentha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:14-15

Futuka pazoipa, nuchite zabwino, funa mtendere ndi kuulondola. Maso a Yehova ali pa olungama mtima, ndipo makutu ake atchereza kulira kwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:14

Ndiye amene akhalitsa malire anu mumtendere; akukhutitsani ndi tirigu wakucha bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:1

Popeza tsono tayesedwa olungama ndi chikhulupiriro, tikhala ndi mtendere ndi Mulungu mwa Ambuye wathu Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:16

Mau a Khristu akhalitse mwa inu chichulukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalimo, ndi mayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuimbira Mulungu ndi chisomo mumtima mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 12:2

Taonani, Mulungu ndiye chipulumutso changa; ndidzakhulupirira, sindidzaopa; pakuti Yehova Mwini ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, Iye ndiye chipulumutso changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:37

Tapenya wangwiro, ndipo taona woongoka mtima! Pakuti ku matsiriziro ake a munthuyo kuli mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:19

Chifukwa chake tilondole zinthu za mtendere, ndi zinthu zakulimbikitsana wina ndi mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:26

Likatha thupi langa ndi mtima wanga, Mulungu ndiye thanthwe la mtima wanga, ndi cholandira changa chosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:15

ndipo mutadziveka mapazi anu ndi makonzedwe a Uthenga Wabwino wa mtendere;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 30:5

Pakuti mkwiyo wake ukhala kanthawi kokha; koma kuyanja kwake moyo wonse. Kulira kuchezera, koma mamawa kuli kufuula kokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:20

Chinyengo chili m'mitima ya oganizira zoipa; koma aphungu a mtendere amakondwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:18

Yehova ali pafupi ndi onse akuitanira kwa Iye, onse akuitanira kwa Iye m'choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 100:4-5

Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko, ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo: Myamikeni; lilemekezeni dzina lake. Pakuti Yehova ndiye wabwino; chifundo chake chimanka muyaya; ndi chikhulupiriko chake ku mibadwomibadwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 65:4

Wodala munthuyo mumsankha, ndi kumyandikizitsa, akhale m'mabwalo anu. Tidzakhuta nazo zokoma za m'nyumba yanu, za m'malo oyera a Kachisi wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:1

Mutonthoze, mutonthoze mtima wa anthu anga, ati Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 131:2

Indedi, ndinalinganiza ndi kutontholetsa moyo wanga; ngati mwana womletsa kuyamwa amake, moyo wanga ndili nao ngati mwana womletsa kuyamwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:13

ndipo muwachitire ulemu woposatu mwa chikondi, chifukwa cha ntchito yao. Khalani mumtendere mwa inu nokha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 18:6

M'kusauka kwanga ndinaitana Yehova, ndipo ndinakuwira Mulungu wanga; mau anga anawamva mu Kachisi mwake, ndipo mkuwo wanga wa pankhope pake unalowa m'makutu mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 24:5

Iye adzalandira dalitso kwa Yehova, ndi chilungamo kwa Mulungu wa chipulumutso chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 26:12

Yehova, mudzatikhazikitsira mtendere; pakuti mwatigwirira ntchito zathu zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 107:29-30

Asanduliza namondwe akhale bata, kotero kuti mafunde ake atonthole. nawasokolotsa kumaiko, kuchokera kum'mawa ndi kumadzulo, kumpoto ndi kunyanja. Pamenepo akondwera, popeza pagwa bata; ndipo Iye awatsogolera kudooko afunako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:7

Njira za munthu zikakonda Yehova ayanjanitsana naye ngakhale adani ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:10

Ndipo Mulungu wa chisomo chonse, amene adakuitanani kulowa ulemerero wake wosatha mwa Khristu, mutamva zowawa kanthawi, adzafikitsa inu opanda chilema mwini wake, adzakhazikitsa, adzalimbikitsa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:7

Ndingakhale ndiyenda pakati pa nsautso, mudzandipatsa moyo; mudzatambasula dzanja lanu pa mkwiyo wa adani anu, ndipo dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 30:18

Chifukwa chake Yehova adzadikira, kuti akukomereni mtima, ndipo chifukwa chake Iye adzakuzidwa, kuti akuchitireni inu chifundo; pakuti Yehova ndiye Mulungu wa chiweruziro; odala ali onse amene amdikira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 31:14-15

Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova, ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga. Nyengo zanga zili m'manja mwanu, mundilanditse m'manja a adani anga, ndi kwa iwo akundilondola ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 9:9

Ndipo Yehova adzakhala msanje kwa iye wokhalira mphanthi. Msanje m'nyengo za nsautso;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 12:6-7

Mau a Yehova ndi mau oona; ngati siliva woyenga m'ng'anjo yadothi, yoiyeretsa kasanu ndi kawiri. Mudzawasunga, Yehova, mudzawatchinjirizira mbadwo uno kunthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 126:5-6

Akubzala ndi misozi adzatuta ndi kufuula mokondwera. Iye amene ayendayenda nalira, ponyamula mbeu yakufesa; adzabweranso ndithu ndi kufuula mokondwera, alikunyamula mitolo yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:9

Koma tisaleme pakuchita zabwino; pakuti pa nyengo yake tidzatuta tikapanda kufooka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:112

Ndinalingitsa mtima wanga uchite malemba anu, kosatha, kufikira chimaliziro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 11:6-9

Mmbulu udzakhala pamodzi ndi mwanawankhosa, ndipo nyalugwe adzagona pansi ndi mwanawambuzi; ndipo mwanawang'ombe ndi mwana wa mkango ndi choweta chonenepa pamodzi; ndipo mwana wamng'ono adzazitsogolera. Ndipo ng'ombe yaikazi ndi chilombo zidzadya pamodzi; ndipo ana ao aang'ono adzagona pansi; ndipo mkango udzadya udzu ngati ng'ombe. Ndipo mwana wakuyamwa adzasewera pa una wa mamba, ndi mwana woleka kuyamwa adzaika dzanja lake m'funkha la mphiri. Sizidzaipitsa, sizidzasakaza m'phiri langa lonse loyera, chifukwa kuti dziko lapansi lidzadzaza ndi odziwa Yehova, monga madzi adzaza nyanja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 62:1-2

Moyo wanga ukhalira chete Mulungu yekha; chipulumutso changa chifuma kwa Iye. Musakhulupirire kusautsa, ndipo musatama chifwamba; chikachuluka chuma musakhazikepo mitima yanu. Mulungu ananena kamodzi, ndinachimva kawiri, kuti mphamvu ndi yake ya Mulungu. Chifundonso ndi chanu, Ambuye, Chifukwa Inu mubwezera munthu aliyense monga mwa ntchito yake. Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; msanje wanga, sindidzagwedezeka kwakukulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:7-8

Pemphani, ndipo chidzapatsidwa kwa inu; funani, ndipo mudzapeza; gogodani, ndipo chidzatsegulidwa kwa inu; pakuti yense wakupempha alandira; ndi wakufunayo apeza; ndi kwa wogogodayo chitsegulidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:21

Musagonje kwa choipa, koma ndi chabwino gonjetsani choipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 127:3-5

Taonani, ana ndiwo cholowa cha kwa Yehova; chipatso cha m'mimba ndicho mphotho yake. Ana a ubwana wake wa munthu akunga mivi m'dzanja lake la chiphona. Wodala munthu amene anadzaza nayo phodo lake: sadzachita manyazi iwo, pakulankhula nao adani kuchipata.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:18

Ndipo musaledzere naye vinyo, m'mene muli chitayiko; komatu mudzale naye Mzimu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 56:3-4

Tsiku lakuopa ine, ndidzakhulupirira Inu. Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ake, ndakhulupirira Mulungu, sindidzaopa; anthu adzandichitanji?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:36-37

Lingitsani mtima wanga kumboni zanu, si ku chisiriro ai. Muchititse mlubza maso anga ndisapenye zachabe, mundipatse moyo mu njira yanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:24

Tsiku ili ndilo adaliika Yehova; tidzasekera ndi kukondwera m'mwemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 57:19

Ndilenga chipatso cha milomo, Mtendere, mtendere kwa iye amene ali kutali, ndi kwa iye amene ali chifupi, ati Yehova; ndipo ndidzamchiritsa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:30

Mtima wabwino ndi moyo wa thupi; koma nsanje ivunditsa mafupa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:7

Wolungama woyenda mwangwiro, anake adala pambuyo pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:3

Achiritsa osweka mtima, namanga mabala ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 26:9

Ndi moyo wanga ndinakhumba Inu usiku; inde ndi mzimu wanga wa mwa ine ndidzafuna Inu mwakhama; pakuti pamene maweruziro anu ali padziko lapansi, okhala m'dziko lapansi adzaphunzira chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:8

Odala ali oyera mtima; chifukwa adzaona Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:28

Koma ine, kundikomera kuyandikiza kwa Mulungu. Ndimuyesa Ambuye Yehova pothawirapo ine, kuti ndifotokozere ntchito zanu zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 128:6

Inde, udzaona zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:30

Kuunika kwa maso kukondweretsa mtima; ndipo pomveka zabwino mafupa amatenga uwisi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:14

Ndipo uku ndi kulimbika mtima kumene tili nako kwa Iye, kuti ngati tipempha kanthu monga mwa chifuniro chake, atimvera;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:33

Ndipo Mulungu wa mtendere akhale ndi inu nonse. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 30:12

kuti ulemu wanga uimbire Inu, wosakhala chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzakuyamikani nthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 20:9

Chikatigwera choipa, lupanga, chiweruzo, kapena mliri, kapena njala, tidzakhala chilili pakhomo pa nyumba iyi, ndi pamaso panu, (pakuti m'nyumba muno muli dzina lanu), ndi kufuulira kwa Inu m'kusauka kwathu; ndipo mudzamvera ndi kulanditsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 18:1-3

Ndikukondani, Yehova, mphamvu yanga. Ndipo anaberekeka pa kerubi, nauluka; nauluka msanga pa mapiko a mphepo. Anaika mdima pobisala pake, hema wake womzinga; mdima wa madzi, makongwa a kuthambo. Mwa kuchezemira kunali pamaso pake makongwa anakanganuka, matalala ndi makala amoto. Ndipo anagunda m'mwamba Yehova, ndipo Wam'mwambamwamba anamvetsa liu lake; matalala ndi makala amoto. Ndipo anatuma mivi yake nawabalalitsa; inde mphezi zaunyinji, nawamwaza. Ndipo zidaoneka zoyendamo madzi, nafukuka maziko a dziko lapansi, mwa kudzudzula kwanu, Yehova, mwa mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwanu. Anatuma kuchokera m'mwamba, ananditenga; anandivuula m'madzi ambiri. Anandipulumutsa ine kwa mdani wanga wamphamvu, ndi kwa iwo ondida ine, pakuti anandiposa mphamvu. Anandipeza ine tsiku la tsoka langa; koma Yehova anali mchirikizo wanga. Ananditulutsanso andifikitse motakasuka; anandilanditsa, pakuti anakondwera ndi ine. Yehova ndiye thanthwe langa, ndi linga langa, ndi Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga, ngaka yanga, ndidzakhulupirira Iye; chikopa changa, nyanga ya chipulumutso changa, msanje wanga. Yehova anandibwezera monga mwa chilungamo changa; anandisudzula monga mwa kusisira kwa manja anga. Pakuti ndasunga njira za Yehova, ndipo sindinachitire choipa kusiyana ndi Mulungu wanga. Pakuti maweruzo ake onse anali pamaso panga, ndipo malemba ake sindinawachotse kwa ine. Ndipo ndinakhala wangwiro ndi Iye, ndipo ndinadzisunga wosachita choipa changa. Ndimo anandisudzulira Yehova monga mwa chilungamo changa, monga mwa kusisira kwa manja anga pamaso pake. Pa wachifundo mukhala wachifundo; pa munthu wangwiro mukhala wangwiro. Pa woyera mtima mukhala woyera mtima; pa wotsutsatsutsa mukhala wotsutsana naye. Pakuti Inu muwapulumutsa anthu aumphawi; koma maso okweza muwatsitsa. Pakuti Inu muyatsa nyali yanga; Yehova, Mulungu wanga, aunikira mdima wanga. Pakuti mwa Inu ndipyola khamu la anthu; ndipo mwa Mulungu wanga ndilumphira linga. Ndidzaitanira Yehova, woyenera kutamandika, ndipo adzandipulumutsa ine kwa adani anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:17

Langiza mwana wako, ndipo adzakupumitsa; nadzasangalatsa moyo wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:50

Chitonthozo changa m'kuzunzika kwanga ndi ichi; pakuti mau anu anandipatsa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:2

Lingalirani zakumwamba osati za padziko ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 16:11

Mudzandidziwitsa njira ya moyo, pankhope panu pali chimwemwe chokwanira; m'dzanja lanu lamanja muli zokondweretsa zomka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:63

Ine ndine wakuyanjana nao onse akukuopani, ndi iwo akusamalira malangizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:24

Ukagona, sudzachita mantha; udzagona tulo tokondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:31

Ndipo tidzatani ndi zinthu izi? Ngati Mulungu ali ndi ife, adzatikaniza ndani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:147-148

Ndinafuula kusanake: ndinayembekezera mau anu. Maso anga anakumana ndi maulonda a usiku, kuti ndilingirire mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:22

Mtima wosekerera uchiritsa bwino; koma mzimu wosweka uphwetsa mafupa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:3

Wodalitsika Mulungu ndiye Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Iye amene, monga mwa chifundo chake chachikulu, anatibalanso ku chiyembekezo cha moyo, mwa kuuka kwa akufa kwa Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 48:18

Mwenzi utamvera malamulo anga mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje, ndi chilungamo chako monga mafunde a nyanja;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 16:5-6

Yehova ndiye gawo la cholowa changa ndi chikho changa, ndinu wondigwirira cholandira changa. Zingwe zandigwera mondikondweretsa; inde cholowa chokoma ndili nacho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 46:5

Mulungu ali m'kati mwake, sudzasunthika, Mulungu adzauthandiza mbandakucha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:1

Taonani, chikondicho Atate watipatsa, kuti titchedwe ana a Mulungu; ndipo tili ife otere. Mwa ichi dziko lapansi silizindikira ife, popeza silimzindikira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 100:1-3

Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi. Tumikirani Yehova ndi chikondwerero: Idzani pamaso pake ndi kumuimbira mokondwera. Dziwani kuti Yehova ndiye Mulungu; Iyeyu anatilenga, ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake ndi nkhosa zapabusa pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 18:30

Mulungu ndiye wangwiro m'njira zake; mau a Yehova ngoyengeka; ndiye chikopa cha onse okhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:19

Koma Mulungu wanga adzakwaniritsa chosowa chanu chilichonse monga mwa chuma chake mu ulemerero mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:52

Ndinakumbukira maweruzo anu kuyambira kale, Yehova, ndipo ndinadzitonthoza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 32:17-18

Ndi ntchito ya chilungamo idzakhala mtendere; ndi zotsata chilungamo zidzakhala mtendere, ndi kukhulupirika kunthawi zonse. Ndipo anthu anga adzakhala m'malo a mtendere, ndi mokhala mokhulupirika ndi mopuma mwa phee.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:28

Ndipo tidziwa kuti amene akonda Mulungu zinthu zonse zithandizana kuwachitira ubwino, ndiwo amene aitanidwa monga mwa kutsimikiza kwa mtima wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:147

Ndinafuula kusanake: ndinayembekezera mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 63:1-3

Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga; ndidzakufunani m'matanda kucha. Moyo wanga ukumva ludzu la kwa Inu, thupi langa lilirira Inu, m'dziko louma ndi lotopetsa, lopanda madzi. Adzawapereka kumphamvu ya lupanga; iwo adzakhala gawo la ankhandwe. Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; yense wakulumbirira iye adzatamandira; pakuti pakamwa pa iwo onena bodza padzatsekedwa. Kuti ndione mphamvu yanu ndi ulemerero wanu, monga ndinakuonani m'malo oyera. Pakuti chifundo chanu chiposa moyo makomedwe ake; milomo yanga idzakulemekezani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 126:1-3

Pobweza Yehova ukapolo wa Ziyoni, tinakhala ngati anthu akulota. Pamenepo pakamwa pathu panadzala ndi kuseka, ndi lilime lathu linafuula mokondwera; pamenepo anati kwa amitundu, Yehova anawachitira iwo zazikulu. Yehova anatichitira ife zazikulu; potero tikhala okondwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 23:6

Inde ukoma ndi chifundo zidzanditsata masiku onse a moyo wanga, ndipo ndidzakhala m'nyumba ya Yehova masiku onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:21

Wolondola chilungamo ndi chifundo apeza moyo, ndi chilungamo, ndi ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:35

Mundiyendetse mopita malamulo anu; pakuti ndikondwera m'menemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:10

Misona ya mkango isowa nimva njala, koma iwo akufuna Yehova sadzasowa kanthu kabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 32:18

Ndipo anthu anga adzakhala m'malo a mtendere, ndi mokhala mokhulupirika ndi mopuma mwa phee.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 9:10

ndipo iwo akudziwa dzina lanu adzakhulupirira Inu; pakuti, Inu Yehova, simunawasiye iwo akufuna Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 1:2

Chisomo kwa inu ndi mtendere za kwa Mulungu Atate wathu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:3

Khulupirira Yehova, ndipo chita chokoma; khala m'dziko, ndipo tsata choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 115:15-16

Odalitsika inu a kwa Yehova, wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi. Kunena za kumwamba, kumwamba ndiko kwa Yehova; koma dziko lapansi analipereka kwa ana a anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 41:10

usaope, pakuti Ine ndili pamodzi ndi iwe; usaopsedwe, pakuti Ine ndine Mulungu wako; ndidzakulimbitsa; inde, ndidzakuthangata; inde, ndidzakuchirikiza ndi dzanja langa lamanja la chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 2:1-5

Mwananga, ukalandira mau anga, ndi kusunga malamulo anga; Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako, moyo wako udzakondwera ndi kudziwa, kulingalira kudzakudikira, kuzindikira kudzakutchinjiriza; kukupulumutsa kunjira yoipa, kwa anthu onena zokhota; akusiya mayendedwe olungama, akayende m'njira za mdima; omwe asangalala pochita zoipa, nakondwera ndi zokhota zoipa; amene apotoza njira zao, nakhotetsa mayendedwe ao. Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi wachiwerewere, kwa mkazi wachilendo wosyasyalika ndi mau ake; wosiya bwenzi la ubwana wake, naiwala chipangano cha Mulungu wake. Nyumba yake itsikira kuimfa, ndi mayendedwe ake kwa akufa; onse akunka kwa iye sabweranso, safika kunjira za moyo; kutcherera makutu ako kunzeru, kulozetsa mtima wako kukuzindikira; nzeru idzakuyendetsa m'njira ya anthu abwino, kuti usunge mayendedwe a olungama. Pakuti oongoka mtima adzakhala m'dziko, angwiro nadzatsalamo. Koma oipa adzalikhidwa m'dziko, achiwembu adzazulidwamo. ukaitananso luntha, ndi kufuulira kuti ukazindikire; ukaifunafuna ngati siliva, ndi kuipwaira ngati chuma chobisika; pompo udzazindikira kuopa Yehova ndi kumdziwadi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:7

Mngelo wa Yehova azinga kuwatchinjiriza iwo akuopa Iye, nawalanditsa iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:6-7

Yehova ndi wanga; sindidzaopa; adzandichitanji munthu? Yehova ndi wanga, mwa iwo akundithandiza; m'mwemo ndidzaona chofuna ine pa iwo akundida.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:20-21

Koma Mulungu wa mtendere amene anabwera naye wotuluka mwa akufa Mbusa wamkulu wa nkhosa ndi mwazi wa chipangano chosatha, ndiye Ambuye wathu Yesu, akuyeseni inu opanda chilema m'chinthu chilichonse chabwino, kuti muchite chifuniro chake; ndi kuchita mwa ife chomkondweretsa pamaso pake, mwa Yesu Khristu; kwa Iyeyu ukhale ulemerero kunthawi za nthawi. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 41:13

Pakuti Ine Yehova Mulungu wako ndidzagwira dzanja lako lamanja, ndi kunena kwa iwe, Usaope ndidzakuthandiza iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:1

Malongosoledwe a mtima nga munthu; koma mayankhidwe a lilime achokera kwa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 78:72

Potero anawaweta monga mwa mtima wake wangwiro; nawatsogolera ndi luso la manja ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 107:20

Atumiza mau ake nawachiritsa, nawapulumutsa ku chionongeko chao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:24

Mudzanditsogolera ndi uphungu wanu, ndipo mutatero, mudzandilandira mu ulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa