Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 34:14 - Buku Lopatulika

14 Futuka pazoipa, nuchite zabwino, funa mtendere ndi kuulondola.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

14 Futuka pazoipa, nuchite zabwino, funa mtendere ndi kuulondola.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

14 Lewa zoipa, ndipo uchite zabwino. Funafuna mtendere ndi kuulondola.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 34:14
26 Mawu Ofanana  

Koma kwa munthu anati, Taonani, kuopa Ambuye ndiko nzeru; ndi kupatukana nacho choipa ndiko luntha.


Ine ndikuti, Mtendere; koma polankhula ine, iwowa akuti, Nkhondo.


Siyana nacho choipa, nuchite chokoma, nukhale nthawi zonse.


Ndinatonthola osanena mau, ndinakhala chete osalawa chokoma; ndipo chisoni changa chinabuka.


Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo, apatutsa kumisampha ya imfa.


Usadziyese wekha wanzeru; opa Yehova, nupatuke pazoipa;


Tasiya m'kamwa mokhota, uike patali milomo yopotoka.


Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa; kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa, ndi m'kamwa mokhota, ndizida.


Odala ali akuchita mtendere; chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.


za Yesu wa ku Nazarete, kuti Mulungu anamdzoza Iye ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu; amene anapitapita nachita zabwino, nachiritsa onse osautsidwa ndi mdierekezi, pakuti Mulungu anali pamodzi ndi Iye.


Ngati nkutheka, monga momwe mukhoza, khalani ndi mtendere ndi anthu onse.


Chikondano chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choipa; gwirizana nacho chabwino.


Pakuti ufumu wa Mulungu sukhala chakudya ndi chakumwa, koma chilungamo, ndi mtendere, ndi chimwemwe mwa Mzimu Woyera.


Chifukwa chake tilondole zinthu za mtendere, ndi zinthu zakulimbikitsana wina ndi mnzake.


Chotsalira, abale, kondwerani. Muchitidwe angwiro; mutonthozedwe; khalani a mtima umodzi, khalani mumtendere; ndipo Mulungu wa chikondi ndi mtendere akhale pamodzi ndi inu.


Chifukwa chake, monga tili nayo nyengo, tichitire onse chokoma, koma makamaka iwo a pa banja la chikhulupiriro.


ndi kuti muyesetse kukhala chete ndi kuchita za inu eni ndi kugwira ntchito ndi manja anu, monga tinakuuzani;


Koma ndithu maziko a Mulungu aimika pokhazikika, ndi kukhala nacho chizindikiro ichi, Ambuye azindikira iwo amene ali ake; ndipo, Adzipatule kwa chosalungama yense wakutchula dzina la Ambuye.


amene anadzipereka yekha m'malo mwa ife, kuti akatiombole ife kuzoipa zonse, nakadziyeretsere yekha anthu akhale ake enieni, achangu pa ntchito zokoma.


Londolani mtendere ndi anthu onse, ndi chiyeretso chimene, akapanda ichi, palibe mmodzi adzaona Ambuye:


Koma musaiwale kuchitira chokoma ndi kugawira ena; pakuti nsembe zotere Mulungu akondwera nazo.


ndipo apatuke pachoipa, nachite chabwino; afunefune mtendere ndi kuulondola.


Wokondedwa, usatsanza chili choipa komatu chimene chili chokoma. Iye wakuchita chokoma achokera kwa Mulungu; iye wakuchita choipa sanamuone Mulungu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa