Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 78:72 - Buku Lopatulika

72 Potero anawaweta monga mwa mtima wake wangwiro; nawatsogolera ndi luso la manja ake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

72 Potero anawaweta monga mwa mtima wake wangwiro; nawatsogolera ndi luso la manja ake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

72 Davide adaŵasamala ndi mtima wolungama, naŵatsogolera ndi dzanja lake mwaluso.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 78:72
15 Mawu Ofanana  

Ndipo Davide anakhala mfumu ya Aisraele onse, Davide naweruza ndi chilungamo milandu ya anthu onse.


chifukwa kuti Davide adachita cholungama pamaso pa Yehova, osapatuka masiku ake onse pa zinthu zonse adamlamulira Iye, koma chokhacho chija cha Uriya Muhiti.


Ndipo Aisraele onse anamva maweruzidwe ake idaweruza mfumu, naopa mfumu; pokhala anaona kuti nzeru ya Mulungu inali mwa iye yakuweruza.


Ndipo iwe ukadzayenda pamaso panga, monga momwe Davide atate wako anayendera ndi mtima woona ndi wolungama, kuzichita zonse ndakulamulirazo, ndi kusunga malemba anga ndi maweruzo anga,


Pakuona nyengo yake ndidzaweruza molunjika.


Wobadwa ndi munthu iwe, Nenera motsutsa abusa a Israele; nenera, nuti nao abusawo, Atero Ambuye Yehova, Tsoka abusa a Israele odzidyetsa okha; kodi abusa sayenera kudyetsa nkhosa?


Ndipo m'mene atamchotsa iye, anawautsira Davide akhale mfumu yao; amenenso anamchitira umboni, nati, Ndapeza Davide, mwana wa Yese, munthu wa pamtima panga, amene adzachita chifuniro changa chonse.


Pakutitu, Davide, m'mene adautumikira uphungu wa Mulungu m'mbadwo mwake mwa iye yekha, anagona tulo, naikidwa kwa makolo ake, naona chivundi;


Uchite changu kudzionetsera kwa Mulungu wovomerezeka, wantchito wopanda chifukwa cha kuchita manyazi, wolunjika nao bwino mau a choonadi.


Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa