Nthaŵi zina, pamakhala mavuto m'moyo wathu, monga matenda. Ndikudziŵa kuti nthaŵi ngati zimenezi zimakhala zovuta komanso zopweteka mtima. Koma kumbukira kuti Mulungu ali nawe.
Iye ali ndi mphamvu zokuchiritsa. Mupemphe Yehova kuti akuchiritse. Mupatse Mulungu ulemu wochokera pansi pa mtima wako.
Pakati pa matenda ndi mavuto, ufuwule kwa Mulungu. Iye akumva ndipo ali wokonzeka kugwira ntchito m'moyo wako. Machiritso adzakufikira, kaya mwachindunji kuchokera kwa Mulungu, kapena kudzera mwa m'bale kapena mlongo amene adzakubweretsera mawu ochiritsa.
Yesu Khristu anatenga kale matenda ndi zowawa zako zonse pa mtanda. Chifukwa cha Yesu, tili ndi mtendere ndi Mulungu, ngakhale m'nthaŵi zovuta. Ika chikhulupiriro chako chonse mwa Yesu. Kudzera m'zilonda zake, umalandira machiritso auzimu. Sitidzamwalira kwamuyaya, ndipo imeneyo ndi mphatso yaikulu kwambiri ya Khristu pa mtanda.
Ambuye akufuna kukupatsa machiritso akuthupi ndi amaganizo, ngakhale tiyenera kumvetereza kuti ndi Iye amene amasankha momwe ndi nthawi yochitira zimenezi. Monga momwe zinalili ndi Bartimeyo wakhungu, Mulungu amafuna kuti timuuze zomwe tikufuna kuti achite. Ndipo kwa Bartimeyo, Yesu anamchiritsa. Iye anati, "Chikhulupiriro chako chakuchiritsa." Ndipo nthawi yomweyo wakhunguyo anayamba kuona.
Mulungu akuyembekezera kuti tiwonetse chikhulupiriro chathu kuti achite chozizwitsa chomwe anakonzeratu kale. Lero, ndikukuuzani kuti muwonjezere chikhulupiriro chanu mwa Mulungu, ndipo musaleke kukhulupirira kuti machiritso anu ali pafupi kuchitika. Ingomupemphani Mulungu. (Yesaya 53:5) “Koma iye analasa chifukwa cha mphulupulu zathu, anaphwanyidwa chifukwa cha zoipa zathu; chilango cha mtendere wathu chinali pa iye, ndipo ndi mikwingwirima yake ife tinachiritsidwa.” Apa mupeza mavesi ambiri okhudza zozizwitsa zomwe Mulungu anachita ndipo adzakulimbitsani chikhulupiriro.
Pa nthaŵiyo nyenyezi zakuvuma zinkaimba pamodzi, ndipo angelo onse a Mulungu ankafuula mokondwa?
Pakamwa panga padzafuula ndi chimwemwe, pamene ndikukuimbirani nyimbo zotamanda. Nawonso mtima wanga umene mwauwombola, udzaimba moyamika.
“Koma perekani nsembe zanu zothokozera kwa Mulungu, ndipo muchite zimene mudalumbira kwa Wopambanazonse.
Ndidzakuyamikani, Inu Mulungu wanga, mfumu yanga, ndidzalemekeza dzina lanu nthaŵi zonse mpaka muyaya.
Chauta, Ambuye athu, dzina lanu ndi lotchuka pa dziko lonse lapansi. Kumwamba amaimba nyimbo zotamanda ulemerero wanu.
Nawonso ana ndi makanda omwe amauimbira. Mwamanga linga chifukwa cha adani anu, kuti mugonjetse onse okuukirani.
Ndimamuuza Chauta kuti, “Inu ndinu Ambuye anga. Ndilibe chinthu china chabwino koma Inu nokha.”
Ndidzapereka kwa Inu nsembe yothokozera, ndidzapemphera potchula dzina la Inu, Chauta.
Ndidzachita zimene ndidalumbira kwa Chauta pamaso pa anthu ake onse.
Ndidzazipereka m'mabwalo a Nyumba ya Mulungu, mu mzinda wa Yerusalemu. Tamandani Chauta!
Zakumwamba zimalalika ulemerero wa Mulungu, thambo limasonyeza ntchito za manja ake.
Zonsezi nzoyenera kuzikhumbira kupambana golide, ngakhale golide wambiri wamtengowapatali, nzotsekemera kupambana uchi, ngakhale uchi wozuna kwambiri.
Malamulo anu amandiwunikira ine mtumiki wanu, poŵasunga ndimalandira mphotho yaikulu.
Nanga ndani angathe kudziŵa zolakwa zake? Inu Chauta, mundichotsere zolakwa zanga zobisika.
Musalole kuti ine mtumiki wanu ndizichimwa dala, kulakwa koteroku ndisakutsate. Tsono ndidzakhala wangwiro wopanda mlandu wa uchimo waukulu.
Mau anga ndi maganizo anga avomerezeke pamaso panu, Inu Chauta, thanthwe langa ndi mpulumutsi wanga.
Usana umasimbira zimenezo usana unzake, usiku umadziŵitsa zimenezo usiku unzake.
Palibe kulankhula, palibe kunena mau aliwonse. Liwu lao silimveka konse.
Komabe uthenga wao umafalikira pa dziko lonse lapansi. Mau aowo amafika mpaka ku mathero a dziko. Mulungu adamangira dzuŵa nyumba m'thambomo.
Anthu akufa sangathe kukutamandani ku manda. M'dziko la akufa ndani angathe kukuyamikani?
Akumanda sangathe kukuyamikani, akufa sangathe kukutamandani. Otsikira ku manda sangathe kukukhulupirirani.
Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasoŵa kanthu.
Amandigoneka pa busa lamsipu. Amanditsogolera ku madzi odikha kokapumulirako.
Amatsitsimutsa moyo wanga. Amanditsogolera m'njira za chilungamo malinga ndi ulemerero wa dzina lake.
Chauta ndiye muuni wanga ndi chipulumutso changa. Ndidzaopa yani? Chauta ndiye linga la moyo wanga, nanga ndichitirenji mantha?
Ndidzatamanda dzina la Mulungu pomuimbira nyimbo, ndidzalalika ukulu wake pomuthokoza.
Zimenezi zidzakondwetsa Chauta kupambana nsembe, ngakhale nsembe ya ng'ombe yamphongo.
Tamandani Chauta, inu okhala kumwamba. Tamandani ulemerero wake ndi mphamvu zake.
Chauta amalamulira nyanja zonse, amakhala kwamuyaya pa mpando wake wachifumu.
Chauta amapatsa anthu ake mphamvu. Amaŵadalitsa anthu ndi mtendere. Salmo la Davide. Nyimbo yoimba potsekula Nyumba ya Mulungu
Tamandani ulemerero wa dzina la Chauta. Mumpembedze mu ulemu wa ungwiro wake.
Kondwerani mwa Chauta, inu anthu ake. Zoonadi ochita zolungama azitamanda.
Zolinga za anthu akunja Chauta amazisandutsa zopandapake. Maganizo ao onse amaŵasandutsa achabechabe.
Koma zolinga za Chauta zimachitika nthaŵi zonse, maganizo a mumtima mwake amakhazikika mpaka muyaya.
Ngwodala mtundu wa anthu amene Mulungu wao ndi Chauta, anthu amene Chauta waŵasankha akeake.
Chauta ali kumwamba, amayang'ana pansi ndi kuwona anthu onse.
Kumene amakhala pa mpando wachifumuko, amapenya anthu onse okhala pa dziko lapansi
Amene amapanga mitima ya anthu onse, ndiye amene amapenya ntchito zao zonse.
Mfumu siipulumuka chifukwa cha kukula kwa gulu lake la ankhondo. Wankhondo sapulumuka chifukwa chakuti ali ndi mphamvu zambiri.
Pa kavalo wankhondo sungaikepo mtima kuti upambane, chifukwa sangathe kupulumutsa munthu, ngakhale kavaloyo ali ndi mphamvu zambiri.
Chauta amayang'ana anthu omumvera, ndi odalira chikondi chake chosasinthika.
Iye amachita izi kuti aŵapulumutse ku imfa ndi kuŵasungira moyo anthuwo pa nthaŵi ya njala.
Tamandani Chauta ndi pangwe. Muimbireni nyimbo ndi zeze wa nsambo khumi.
Mitima yathu ikuyembekeza Chauta, chifukwa Iye ndiye chithandizo ndi chishango chathu.
Mitima yathu imasangalala mwa Chauta, popeza kuti timadalira dzina lake loyera.
Inu Chauta, chikondi chanu chosasinthika chikhale pa ife, chifukwa timakhulupirira Inu.
Muimbireni nyimbo yatsopano, kodolani nsambozo mwaluso ndi kufuula mosangalala.
Ndimatambalitsira manja anga kwa Inu, mtima wanga umamva ludzu lofuna Inu, monga limachitira dziko louma.
Ndidzayamika Chauta nthaŵi zonse, pakamwa panga padzatamanda Iye kosalekeza.
Ngakhale anaamkango amasoŵa chakudya ndipo amakhala anjala, koma anthu amene amalakalaka Chauta, sasoŵa zinthu zabwino.
Bwerani ana anga, mundimvere, ndidzakuphunzitsani kuwopa Chauta.
Ndani mwa inu amakhumba moyo ndi kulakalaka kuti akhale masiku ambiri, kuti asangalale ndi zinthu zabwino?
Ngati ufunadi moyo, usalankhule zoipa, pakamwa pako pasakambe zonyenga.
Lewa zoipa, ndipo uchite zabwino. Funafuna mtendere ndi kuulondola.
Ngati mumvera Chauta, adzakuyang'anirani ndipo adzayankha kupempha kwanu.
Koma Chauta amaŵakwiyira anthu ochita zoipa, anthuwo sadzakumbukikanso pansi pano.
Pamene anthu ake akulira kuti aŵathandize, Chauta amamva naŵapulumutsa m'mavuto ao onse.
Chauta amakhala pafupi ndi anthu a mtima wosweka, amapulumutsa otaya mtima.
Anthu a Mulungu amaona masautso ambiri. Komabe Chauta amawapulumutsa m'mavuto awo onse.
Moyo wanga umanyadira Chauta. Anthu ozunzika amve ndipo akondwere.
Chauta amasunga thupi la munthuyo, palibe fupa limene limasweka.
Choipa chitsata mwini, anthu odana ndi munthu wa Mulungu adzalangidwa.
Chauta amaombola moyo wa atumiki ake. Palibe wothaŵira kwa Iye amene adzalangidwe.
Lalikani pamodzi nane ukulu wa Chauta, tiyeni limodzi tiyamike dzina lake.
Monga momwe mbaŵala imakhumbira mtsinje wamadzi, ndimo m'mene mtima wanga umakhumbira Inu Mulungu wanga.
Kunyoza kwa adani anga kumandipweteka ngati bala lofa nalo la m'thupi mwanga, akamandifunsa nthaŵi zonse kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika choncho m'kati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamtamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.
Mtima wanga ukumva ludzu lofuna Mulungu, Mulungu wamoyo. Kodi ndidzafika liti pamaso pa Mulungu?
Ndidzakuthokozani, Inu Chauta, ndi mtima wanga wonse. Ndidzasimba za ntchito zanu zonse zodabwitsa.
“Khalani chete, ndipo mudziŵe kuti ndine Mulungu. Mitundu ya anthu imanditamanda, a m'dziko lapansi amandiyamika.”
Ombani m'manja inu anthu a mitundu yonse. Fuulani kwa Mulungu poimba nyimbo zachimwemwe.
Paja Chauta Wopambanazonse, ndi woopsa, ndiye mfumu yaikulu pa dziko lonse lapansi.
Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, ndimakufunafunani. Mtima wanga ukumva ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka Inu ngati dziko louma, loguga ndi lopanda madzi.
Iwo adzaperekedwa kuti akaphedwe ku nkhondo, motero adzasanduka chakudya cha nkhandwe.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu. Onse olumbirira Iye, adzamtamanda, koma pakamwa pa anthu abodza padzatsekedwa.
Ndikukhumbira kukuwonani m'malo anu oyera ndi kuwona mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
Ndidzakutamandani chifukwa chikondi chanu nchabwino kupambana moyo.
Choncho ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga. Ndidzakweza manja anga kwa Inu mopemphera.
Malo amene mumakhalamo, Inu Chauta Wamphamvuzonse, ndi okoma kwambiri.
Kukhala tsiku limodzi m'mabwalo anu nkwabwino kwambiri kupambana kukhala masiku ambiri kwina kulikonse. Nkadakonda kukhala wapakhomo wa Nyumba ya Mulungu wanga kupambana kukhala m'nyumba za anthu oipa.
Pakuti Chauta ndiye dzuŵa ndi chishango, amatichitira chifundo ndi kutipatsa ulemu. Chauta saŵamana zabwino anthu oyenda molungama.
Inu Chauta Wamphamvuzonse, ngwodala munthu woika chikhulupiriro chake pa Inu.
Mtima wanga ukulakalaka, mpaka kukomoka, kufunitsitsa kuwona mabwalo a Chauta. Inu Mulungu wamoyo, ndikukuimbirani mwachimwemwe ndi mtima wanga wonse.
Inu Ambuye, ndinu kothaŵira kwathu pa mibadwo yonse.
Zaka za moyo wathu nzokwanira makumi asanu ndi aŵiri, tikakhala amphamvu, ndiye makumi asanu ndi atatu. Koma zaka zonsezo ndi za nkhaŵa ndi mavuto. Zakazo zimatha msanga, ife nkumapita.
Kodi ndani amadziŵa kukula kwa mkwiyo wanu ndi ukali wanu, kupambana anthu okuwopani?
Tsono tiphunzitseni kuŵerenga masiku athu, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
Lezani mtima, Inu Chauta. Nanga mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
Tidzazeni m'maŵa mulimonse ndi chikondi chanu chosasinthika, kuti tizikondwa ndi kusangalala masiku athu onse.
Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mudatisautsira, zaka zambiri monga zaka zimene tidaona mavuto.
Mulole kuti ntchito zanu ziwoneke kwa atumiki anu, mphamvu zanu zaulemerero ziwoneke kwa ana ao.
Inu Ambuye, Mulungu wathu, mutikomere mtima, ndi kudalitsa zonse zimene timachita, ndithu mudalitse ntchito zonse za manja athu.
Mapiri asanabadwe, ndipo musanalenge dziko lapansi ndi pokhala anthu, ndinu Mulungu kuyambira muyaya mpaka muyaya.
Bwerani, timuimbire Chauta. Tiyeni tifuule ndi chimwemwe kwa Iye, thanthwe lotipulumutsa.
Pa zaka makumi anai ndidaipidwa ndi mbadwo umenewo, choncho ndidati, “Ameneŵa ndi anthu osakhulupirika, sasamalako njira zanga.”
Choncho ndidakwiya nkulumbira kuti anthuwo sadzaloŵa ku malo anga ampumulo.
Tiyeni, tikafike pamaso pake, tikamthokoze, tiyeni tifuule kwa Iye ndi chimwemwe, timuimbire nyimbo zotamanda.
Pakuti Chauta ndiye Mulungu wamkulu, ndiye Mfumu yaikulu yopambana milungu yonse.
Imbirani Chauta nyimbo yatsopano! Imbirani Chauta, anthu a m'dziko lonse lapansi!
Uzani mitundu ya anthu kuti, “Chauta ndiye Mfumu. Dziko lonse lidakhazikitsidwa molimba, silidzagwedezeka konse. Adzaweruza mitundu yonse ya anthu mwachilungamo.”
Zakumwamba zisangalale, zapansi pano zikondwere, nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zam'menemo.
Minda zikondwe pamodzi ndi zonse zam'menemo. Mitengo yam'nkhalango idzaimba mokondwa
pamaso pa Chauta, pamene zabwera kudzalamulira dziko lapansi. Adzalamulira dziko lonse mwachilungamo, adzalamulira anthu a mitundu yonse moona.
Imbirani Chauta, tamandani dzina lake! Lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Lengezani za ulemerero wake kwa anthu a mitundu yonse, simbani za ntchito zake zodabwitsa kwa anthu a m'maiko onse.
Chauta ngwamkulu, ngwoyenera kumtamanda kwambiri. Nwoyenera kumuwopa kupambana milungu yonse.
Fuulirani Chauta ndi chimwemwe, inu dziko lonse lapansi. Muimbireni mokondwa nyimbo zotamanda.
Imbani nyimbo zoyamika Chauta ndi pangwe, lizani pangwe ndi nyimbo zokoma.
Imbirani Chauta Mfumu, imbani molimbika ndi malipenga ndi mbetete.
Fuulani kwa Chauta ndi chimwemwe, inu maiko onse.
Tumikirani Chauta mosangalala. Bwerani pamaso pake mukuimba mokondwa.
Dziŵani kuti Chauta ndiye Mulungu. Ndiye amene adapanga ife, ndipo ifeyo ndife ake. Ndife anthu ake, nkhosa za busa lake.
Loŵani pa zipata zake mukuthokoza, pitani m'mabwalo a Nyumba yake mukutamanda. Yamikani Chauta, lemekezani dzina lake!
Paja Iye ndi wabwino. Chikondi chake nchamuyaya, kukhulupirika kwake nkosatha.
Tamanda Chauta, iwe mtima wanga, moyo wanga wonse umuyamike potchula dzina lake loyera.
Satilanga moyenerera machimo athu, satibwezera molingana ndi zolakwa zathu.
Monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, ndi momwenso chidakulira chikondi chake chosasinthika kwa anthu oopa Chauta.
Monga kuvuma kuli kutali ndi kuzambwe, ndi momwenso amachotsera zolakwa zathu kuti zikhale kutali ndi ife.
Monga bambo amachitira chifundo ana ake, ndi momwenso Chauta amaŵachitira chifundo omulemekeza.
Amadziŵa m'mene adatipangira, amakumbukira kuti ife ndife fumbi.
Kunena za munthu, masiku ake sakhalitsa, ali ngati a udzu, munthuyo amakondwa ngati duŵa lakuthengo.
Koma mphepo ikaombapo, duŵalo pamakhala palibe, siliwonekanso pa malo ake.
Koma chikondi cha Chauta nchamuyaya kwa anthu omumvera, zidzukulu zao zonse amazichitira zolungama.
Anthuwo ndi amene amasunga chipangano chake, amene amakumbukira kusunga malamulo ake.
Chauta wakhazikitsa mpando wake wachifumu kumwamba, ndipo amalamulira zonse mu ufumu wake.
Tamanda Chauta, iwe mtima wanga, ndipo usaiŵale zabwino zake zonse.
Tamandani Chauta, inu angelo ake, inu amphamvu amene mumamva mau ake, amene mumachita zimene amalamula.
Tamandani Chauta, inu magulu a ankhondo ake onse, atumiki ake ochita zimene Iye afuna.
Tamandani Chauta, inu zolengedwa zake zonse, ku madera onse a ufumu wake. Nawenso mtima wanga, tamanda Chauta!
Ndiye amene amakhululukira machimo ako onse, ndi kuchiritsa matenda ako onse.
Ndiye amene amapulumutsa moyo wako ku manda. Amakuveka chikondi chake chosasinthika ndiponso chifundo chake ngati chisoti chaufumu.
Ndiye amene amakupatsa zabwino nthaŵi zonse za moyo wako, choncho umakhalabe wa mphamvu zatsopano ngati mphungu.
Tamanda Chauta, iwe mtima wanga. Inu Chauta, Mulungu wanga, ndinu aakulu kwambiri. Mumavala ulemu ndi ufumu.
Inu mumatumphutsa akasupe m'zigwa, mitsinje imayenda pakati pa mapiri.
Imapatsa nyama zonse zakuthengo madzi akumwa, mbidzi zimapherapo ludzu.
Mbalame zimamanga zisa pafupi ndi mitsinjeyo, zimaimba m'nthambi za mitengo.
Inu mumathirira mapiri ndi madzi ochokera ku malo anu akumwamba. Dziko lapansi ladzaza ndi madalitso anu.
Mumameretsa udzu kuti ng'ombe zidye, ndi zomera kuti munthu azilima ndi kupeza chakudya m'nthaka.
Amapezamo vinyo wosangalatsa mtima wake, mafuta odzola kuti thupi lake lisisire, ndiponso buledi kuti ampatse mphamvu.
Mitengo ya Chauta amaithirira ndi madzi ambiri, mikungudza ya ku Lebanoni imene adaibzala.
Mbalame zimamanga zisa m'menemo, dokowe amamanga chisa m'mikungudzamo.
M'mapiri aatali ndimo m'mene mumakhala mbalale, m'matanthwe ndimo m'mene mumathaŵira mbira.
Inu mudapanga mwezi kuti uzisiyanitsa nyengo, ndipo dzuŵa limadziŵa nthaŵi yake yoloŵera.
Mumadzifunditsa ndi kuŵala ngati chovala, mwatambasula mlengalenga ngati hema.
Thokozani Chauta, tamandani dzina lake, lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.
Lonjezolo adabwerezanso kwa Yakobe kuti likhale chipangano chokhazikika mu Israele mpaka muyaya.
Adati, “Ndidzakupatsa dziko la Kanani kuti likhale choloŵa chako chokhalira iweyo.”
Pamene anali anthu oŵerengeka, anthu osatchuka, ongokhala nawo m'dzikomo,
omangoyendayenda kuchokera ku mtundu wina wa anthu kupita ku mtundu wina, kuchokera ku ufumu wina kupita ku ufumu wina,
sadalole ndi mmodzi yemwe kuti aŵapsinje, adalanga mafumu ena chifukwa cha anthu akewo.
Adati, “Musakhudze odzozedwa anga, musaŵachite choipa aneneri anga.”
Pamene Chauta adadzetsa njala m'dziko la Kanani ndi kuwononga chakudya chonse,
Iye anali atatuma munthu patsogolo pa anthu ake, Yosefe uja amene adagulitsidwa ngati kapolo.
Mapazi ake adapwetekedwa ndi matangadza, khosi lake lidavekedwa unyolo,
mpaka zimene Yosefe adanena zija zidachitikadi. Mau a Chauta adatsimikiza kuti iye sadalakwe.
Imbirani Chauta, muimbireni nyimbo zomtamanda, lalikani za ntchito zake zodabwitsa.
Motero mfumu idalamula kuti akammasule, wolamulira mitundu ya anthuyo adammasuladi.
Adamsandutsa mbuye wa nyumba yake, ndi wolamulira chuma chake chonse,
kuti azilangiza nduna zake monga momwe ankafunira, ndi kuŵaphunzitsa nzeru akuluakulu.
Tsono Israele adafika ku Ejipito. Yakobeyo adakhala nawo m'dziko la Hamu.
Chauta adalola kuti anthu ake achuluke, naŵasandutsa amphamvu kupambana adani ao.
Adaumitsa mitima ya adaniwo kuti adane ndi anthu ake ndi kuŵapanganirana zaupandu.
Kenaka adatuma Mose mtumiki wake pamodzi ndi Aroni amene adamsankha.
Iwo adachita zizindikiro m'dzina lake pakati pa anthuwo, adachita ntchito zozizwitsa m'dziko la Hamu.
Chauta adatumiza mdima, nasandutsa dzikolo kuti likhale lamdima. Komabe anthuwo adakaniratu mau a Chauta.
Iye adasandutsa madzi ao kukhala magazi, ndipo nsomba zao zidafa.
Munyadire dzina lake loyera. Ikondwe mitima ya anthu amene amapembedza Chauta.
Dziko lao lidadzaza ndi achule, ngakhale m'zipinda za mafumu zomwe.
Adalankhula, ndipo kudatuluka ntchentche zochuluka, mtundu wa udzudzu udaloŵa m'dziko mwao monse.
Adaŵagwetsera matalala m'malo mwa mvula, adaŵagwetsera ching'aning'ani chimene chinkang'anima m'dziko mwao monse.
Adagwetsa mipesa yao ndi mikuyu yao, adathyola mitengo yonse ya m'dziko mwao.
Adalankhula, ndipo kudafika dzombe ndi mandowa osaŵerengeka,
amene adaononga zomera zonse za m'dziko mwao, nadya zipatso zonse za m'minda mwao.
Iye adapha ana onse achisamba m'dziko mwao, ana onse oyamba, oŵabala akadali abiriŵiri.
Kenaka Chauta adaŵatulutsa Aisraele atatenga siliva ndi golide, pakati pa mafuko awo panalibe amene adafooka.
Aejipito adasangalala pamene iwo adapita, chifukwa ankachita nawo mantha anthuwo.
Chauta adaika mtambo kuti uziphimba anthu ake, adaika moto kuti uziŵaunikira usiku.
Muzidalira Chauta ndi mphamvu zake. Muziyesetsa kukhala pamaso pake kosalekeza.
Tamandani Chauta! Mtamandeni, inu atumiki ake, tamandani dzina la Chauta.
Yamikani Chauta kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Dzina la Chauta litamandike kuyambira ku matulukiro a dzuŵa mpaka ku maloŵero ake.
Chauta akulamulira anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi waukulu kuposa wa mlengalenga.
Tamandani Chauta, inu mitundu yonse ya anthu. Mlemekezeni kwambiri, inu anthu a m'maiko onse.
Pakuti chikondi chake kwa ife nchachikulu, kukhulupirika kwa Chauta nkwamuyaya. Tamandani Chauta!
hokozani Chauta chifukwa ngwabwino, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Adapha ana achisamba a ku Ejipito, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Ndipo adatulutsa Aisraele pakati pao, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Ndi dzanja lamphamvu ndi mkono wotambalitsa, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Adagaŵa pakati Nyanja Yofiira, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Adaolotsa Aisraele pakati pake, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Koma adamiza Farao ndi ankhondo ake m'Nyanja Yofiira, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Adatsogolera anthu ake m'chipululu, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Adapha mafumu amphamvu, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Adaphanso mafumu otchuka, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Adapha Sihoni, mfumu ya Aamori, pakuti chikondi chake nchamuyaya,
Thokozani Mulungu wa milungu, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Adapha Ogi, mfumu ya ku Basani, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Napereka dziko la mafumuwo kuti likhale choloŵa, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Choloŵa cha Israele mtumiki wake, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Adatikumbukira pamene adani adatigonjetsa, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Ndipo adatipulumutsa kwa adani athu, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Amapatsa zamoyo zonse chakudya, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Thokozani Mulungu wakumwamba, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Thokozani Chauta woposa ambuye onse, pakuti chikondi chake nchamuyaya.
Chauta mwafufuzafufuza, ndipo mwandidziŵa.
ngakhale kumenekonso mudzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandichirikiza.
Ndikanena kuti, “Mdima undiphimbe, kuŵala kumene kwandizinga kusanduke mdima,”
ngakhale mdimawo, kwa Inu si mdima konse, kwa Inu usiku umaŵala ngati usana, mdima uli ngati kuŵala.
Paja ndinu mudapanga za m'kati mwanga, mudandiwumba m'mimba mwa amai anga.
Ndikukutamandani, Inu oopsa ndi odabwitsa. Ntchito zanu zonse nzodabwitsa. Mumandidziŵa bwino kwambiri.
Mapangidwe anga sadabisike pamaso panu pamene ndinkapangidwa mwachinsinsi, pamene ndinkaumbidwa mwaluso m'mimba mwa amai anga.
Maso anu adandiwona ndisanabadwe. Masiku a moyo wanga mudaŵalemberatu m'buku mwanu, asanayambe nkuŵerengedwa komwe.
Maganizo anu, Inu Mulungu, ndi ozama kwa ine, ndi osaŵerengeka konse.
Ndikadaŵaŵerenga, bwenzi ali ambiri koposa mchenga. Ndikamadzuka ndimakhala nanube.
Ndikadakonda kuti muwononge anthu oipa, Inu Mulungu, ndipo kuti anthu okhetsa magazi andichokere.
Inu mumadziŵa pamene ndikhala pansi, pamenenso ndidzuka, mumazindikira maganizo anga muli kutali.
Anthuwo amakunenani zinthu zoipa, namakuukirani ndi mtima woipa.
Kodi sindidana nawo anthu odana nanu, Inu Chauta? Kodi sindinyansidwa nawo anthu okuukirani?
Ndimadana nawo ndi chidani chenicheni. Ndimaŵayesa adani anga.
Fufuzeni, Inu Mulungu, kuti mudziŵe mtima wanga. Yeseni kuti mudziŵe maganizo anga.
Muwone ngati ndimatsata njira yoipa iliyonse, ndipo munditsogolere m'njira yanu yamuyaya.
Mumandipenyetsetsa ndikamayenda ndiponso ndikamagona, mumadziŵa njira zanga zonse.
Ngakhale mau anga asanafike pakamwa panga, Inu Chauta mumaŵadziŵa onse.
Paja ndinu mudapanga za m'kati mwanga, mudandiwumba m'mimba mwa amai anga.
Ndikukutamandani, Inu oopsa ndi odabwitsa. Ntchito zanu zonse nzodabwitsa. Mumandidziŵa bwino kwambiri.
Ndidzakuyamikani, Inu Mulungu wanga, mfumu yanga, ndidzalemekeza dzina lanu nthaŵi zonse mpaka muyaya.
Zamoyo zonse zidzakuthokozani, Inu Chauta, anthu anu onse oyera mtima adzakutamandani.
Adzalankhula za ulemerero wa ufumu wanu, adzasimba za mphamvu zanu,
kuti adziŵitse anthu onse za ntchito zanu zamphamvu, kutinso asimbe za ulemerero ndi za ufumu wanu waukulu.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ulamuliro wanu ndi wa pa mibadwo yonse. Chauta ndi wokhulupirika pa mau ake onse, ndi wokoma mtima pa zochita zake zonse.
Chauta amachirikiza onse ogwa m'mavuto, amakweza onse otsitsidwa.
Maso onse amayang'anira kwa Inu, ndipo mumaŵapatsa chakudya pa nthaŵi yake.
Mumafumbatula dzanja lanu, ndipo mumapatsa chamoyo chilichonse zofuna zake.
Chauta ndi wolungama m'zochita zake zonse, ndi wachifundo pa zonse zimene achita.
Chauta ali pafupi ndi onse amene amamutama mopemba. Ali pafupi ndi onse amene amamutama mokhulupirika.
Amene amamvera Chauta, amaŵapatsa zofuna zao, amamvanso kulira kwao, naŵapulumutsa.
Ndidzakuthokozani tsiku ndi tsiku, ndidzatamanda dzina lanu mpaka muyaya.
Onse amene amakonda Chauta, amaŵasunga, koma Chauta adzaononga oipa onse.
Pakamwa panga padzayamika Chauta, zamoyo zonse zitamande dzina lake loyera mpaka muyaya.
Chauta ndi wamkulu ndi woyenera kumtamanda kwambiri, ndipo ukulu wake sitingathe kuumvetsa.
Tamandani Chauta! Tamanda Chauta, iwe mtima wanga.
Chauta adzakhala mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako, iwe Ziyoni, adzalamulira ku mibadwo yonse. Tamandani Chauta!
Ndidzatamanda Chauta pa moyo wanga wonse. Ndidzaimba nyimbo zotamanda Mulungu wanga nthaŵi zonse pamene ndili moyo.
Tamandani Chauta! Nkwabwino kuimba nyimbo zotamanda Mulungu wathu, nkokondwetsa mtima kumtamanda moyenera.
Tamandani Chauta! Tamandani Chauta inu okhala kumwamba, mtamandeni inu okhala mu mlengalenga!
Inu nyama zakutchire ndi zoŵeta zonse, inu zinthu zokwaŵa ndi mbalame zouluka!
Inu mafumu a pa dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse, inu akuluakulu ndi olamulira dziko lapansi!
Inu anyamata pamodzi ndi anamwali, inu nkhalamba ndi ana omwe!
Onsewo atamande dzina la Chauta, pakuti dzina lake lokha nlolemekezeka, ulemerero wake ndi woposa, pansi pano nkumwamba komwe.
Chauta wakweza anthu ake poŵapatsa mphamvu. Walemekeza anthu ake onse oyera mtima, Aisraele amene Iye amaŵakonda. Tamandani Chauta!
Mtamandeni inu angelo ake onse, mtamandeni inu magulu a ankhondo ake onse!
Mtamandeni inu dzuŵa ndi mwezi, mtamandeni inu nonse nyenyezi zoŵala!
Mtamandeni inu thambo lakumwambamwamba, ndi inu madzi a pamwamba pa thambo!
Zonsezo zitamande dzina la Chauta! Paja Iye adaalamula, izo nkulengedwa.
Tamandani Chauta! Tamandani Mulungu m'malo ake opatulika. Mtamandeni ku thambo lake lamphamvu.
Mtamandeni chifukwa cha ntchito zake zamphamvu, mtamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
Mtamandeni pomuimbira lipenga, mtamandeni ndi gitara ndi zeze.
Mtamandeni poimba ng'oma ndi povina, mtamandeni ndi zipangizo zansambo ndi mngoli.
Mtamandeni ndi ziwaya zamalipenga zolira, mtamandeni ndi ziwaya zamalipenga zolira kwambiri.
Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Chauta. Tamandani Chauta!
Tsono Mose pamodzi ndi Aisraele aja adaimba nyimbo iyi, kuimbira Chauta, adati, “Ndidzaimbira Chauta chifukwa choti wapambana, waponya m'nyanja akavalo pamodzi ndi okwerapo omwe.
Koma Inu mudangouzira ndi mphepo yanu, ndipo nyanja idaŵamiza. Adangomira ngati chitsulo mpaka pansi pa madzi.
“Inu Chauta, kodi pali mulungu wina wofanafana nanu? Ndani amafanafana ndi Inu, amene muli aulemu chifukwa cha ungwiro wanu? Ndani amafanafana nanu, Inu amene muli oopsa chifukwa cha ntchito zanu zaulemu ndi zodabwitsa?
Mudatambalitsa dzanja lanu lamanja, ndipo nthaka idaŵameza.
“Koma anthu amene mudaŵaombola, mudaŵatsogolera ndi chikondi chanu chosasinthika. Mudaŵatsogolera ku malo anu oyera ndi mphamvu zanu.
Anthu a mitundu ina amva mbiriyi, ndipo anjenjemera ndi mantha. Mantha oopsa aŵagwira Afilisti.
Tsopano lino mafumu a ku Edomu ataya mtima. Atsogoleri a ku Mowabu ayambapo kunjenjemera. Onse a ku Kanani agooka m'nkhongono.
Onsewo agwidwa ndi mantha oopsa. Iwo akhala chete ngati mwala, chifukwa cha kuwopa mphamvu zanu zazikulu. Angokhala chete mpaka anthu anu, Inu Chauta, atabzola, anthu amene mudaŵaombola mu ukapolo.
Mudzaŵaloŵetsa ndi kuŵakhazika pa phiri lanu, pa malo amene Inu Chauta mudaŵapanga kuti akhale anu, m'nyumba yopembedzera imene Inu mudaimanga.
Chauta adzakhala mfumu mpaka muyaya.”
Pamene akavalo a Farao, pamodzi ndi magaleta ndi okwerapo ake omwe, adaloŵa m'nyanja, Chauta adaŵabweza madziwo, ndipo adamiza onsewo. Koma Aisraele adayenda pouma m'kati mwa nyanjayo.
Chauta ndiye mphamvu zanga, ndiye amene ndimamuimbira, ndiye chipulumutso changa. Iye ndiye Mulungu wanga, ndipo ndidzamtamanda. Ndiye Mulungu wa atate anga, ndipo ndidzamuyamika kwakukulu.
Hana adapemphera nati, “Mtima wanga ukukondwa chifukwa cha zimene Chauta wandichitira, Ndikuyenda ndi mdidi chifukwa cha Chauta. Pakamwa panga pakula nkuseka adani anga monyodola. Ndakondwa kwambiri chifukwa mwandipulumutsa.
Chauta adzatswanya adani ake, adzaŵaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba. Chauta adzaŵaweruza mpaka ku mathero a dziko lapansi. Koma adzalimbikitsa mfumu yake, adzakuza mphamvu za wodzozedwa wake.”
Tsono Elikana adabwerera kwao ku Rama. Koma mnyamata uja Samuele adatsala, ndipo ankatumikira Chauta pamaso pa wansembe Eli.
Tsono ana a Eli anali achabechabe, sankasamalako za Chauta.
Sankasamalanso za khalidwe loyenera ansembe pakati pa anthu. Ankachita motere: pamene munthu wina ankapereka nsembe, nyama ilikuŵira pa moto, mtumiki wake wa wansembe ankabwera, atatenga chiforoko cha mano atatu.
Ankachipisa mu mphika, ndipo zonse zimene chiforoko chija chinkajinya, wansembe ankatenga kuti zikhale zake. Aisraele onse amene ankafika ku Silo, ana a Eli ankaŵachita mokhamokhamo.
Kuwonjezera apo, mafuta asanatenthedwe, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi kuuza munthu wopereka nsembeyo kuti, “Patse nyama yoti ndikaotchere wansembe. Pakuti sadzalandira nyama yophika, koma yosaphika.”
Ndipo munthuyo akanena kuti, “Apserezeretu mafutaŵa poyamba, pambuyo pake ndiye mutenge monga momwe mufunira,” mtumiki uja ankati, “Iyai, patsiretu tsopano pompano. Ngati sutero, ndichita kukulanda.”
Motero tchimo la ana a Eli linali lalikulu pamaso pa Chauta, pakuti ankanyoza nsembe za Chauta.
Samuele pa unyamata wake ankatumikira pamaso pa Chauta, atavala efodi yabafuta.
Chaka chilichonse mai wake ankamsokera mkanjo, ndi kukampatsa pamene ankapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe ya chaka ndi chaka.
“Palibe woyera wina wofanafana ndi Chauta, palibe wina koma Iye yekha. Palibe thanthwe lina lotchinjiriza lofanafana ndi Mulungu wathu.
Uzikhulupirira Chauta ndi mtima wako wonse, usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Pa ntchito zako zonse uzivomera kuti kuli Mulungu, choncho njira zako Iye adzazilungamitsa.
Aserafiwo ankafuulirana kuti, “Ngwoyera, ngwoyera, ngwoyera Chauta Wamphamvuzonse, ulemerero wake wadzaza dziko lonse lapansi.”
“Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga, ndidzamkhulupirira Iye, ndipo sindidzaopa. Pakuti Chauta ndiye mphamvu zondilimbitsa, ndiye amene ndimamuimbira, ndiye Mpulumutsi wanga.”
Mudzakondwera pokatunga madzi m'zitsime za chipulumutso.
Tsiku limenelo mudzati: “Thokozani Chauta, tamandani dzina lake. Mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
“Imbirani Chauta nyimbo zotamanda, pakuti wachita zazikulu. Zimenezi zidziŵike pa dziko lonse lapansi.
Inu Chauta, ndinu Mulungu wanga. Ndidzakulemekezani ndi kutamanda dzina lanu. Pakuti mwachita zinthu zodabwitsa mokhulupirika ndi motsimikiza, zinthu zimene mudakonzeratu kalekale.
Kodi sudziŵa? Kodi sudamve? Chauta ndiye Mulungu wachikhalire, Mlengi wa dziko lonse lapansi. Satopa kapena kufooka, palibe amene amadziŵa maganizo ake.
Amalimbitsa ofooka, ndipo otopa amaŵaonjezera mphamvu.
Kukumveka mau akuti, “Konzani njira ya Chauta m'thengo, lungamitsani mseu wa Mulungu wathu m'chipululu.
Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufooka, ngakhale anyamata amaphunthwa ndi kugwa.
Koma amene amakhulupirira Chauta adzalandira mphamvu zatsopano, adzauluka ngati ziwombankhanga. Adzathamanga koma osatopa, adzayenda koma osalefuka konse.
Imbirani Chauta nyimbo yatsopano. Mtamandeni, inu okhala m'dziko lonse lapansi! Mtamandeni, inu zolengedwa zonse zam'nyanja. Imbani, inu maiko akutali ndi onse okhala kumeneko.
Chipululu ndi mizinda yake zitamande Mulungu. Midzi ya Akedara imuyamike. Okhala mu mzinda wa Sela amuimbire mokondwa, afuule pa nsonga za mapiri.
Atamande Chauta, ndipo alalike ulemu wake ku maiko akutali.
Koma tsopano Chauta amene adakulenga iwe Yakobe, amene adakuumba iwe Israele, akunena kuti, “Usaope, chifukwa ndidakuwombola, ndidachita kukutchula dzina lako, ndiwe wanga.
Inu Aisraele, ndinu mboni zanga, ndinu atumiki anga amene ndidakusankhulani, kuti mundidziŵe ndi kundikhulupirira, ndipo mumvetse kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipadapangidwepo mulungu wina, ndipo pambuyo panga sipadzakhalanso wina.
Chauta ndi Ineyo, mpulumutsi wanu ndine ndekha.
Ndine amene ndidaneneratu zimenezi, ndipo ndine ndidakupulumutsani. Si mulungu wina wachilendo amene adazichita pakati pa inu. Inu nomwe ndinu mboni zanga, ndikutero Ine Chauta.
Ine ndine Mulungu ndipo ndidzakhalapo nthaŵi zonse. Palibe amene angathe kuthaŵa m'manja mwanga, palibe amene angathe kusintha zochita zanga.”
Chauta, Momboli wanu, Woyera uja wa Israele, akunena kuti, “Ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babiloni, kuti ndikupulumutseni. Ndidzagwetsa zipata za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
Ine ndine Chauta, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israele. Ine ndekha ndine mfumu yanu.”
Kale lija Chauta adapanga njira pa nyanja, njira pakati pa madzi amphamvu.
Adasonkhanitsa magaleta ndi akavalo, ndiponso gulu lankhondo ndi asirikali amphamvu. Onsewo adagwa osadzukanso, adazimitsidwa ndi kutheratu ngati chingwe cha nyale.
Iyeyo akunena kuti, “Musakumbukire zakale kapena kumaganiziranso zinthu zimene zidachitika kale.
Ndikuchita zinthu zatsopano. Zayamba kale kuwoneka, kodi simukuzipenya? Ndikulambula mseu m'chipululu, ndipo ndikukupatsani mitsinje m'dziko louma.
Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe, pamene ukuwoloka mitsinje, siidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto sudzapsa, malaŵi ake sadzakutentha.
“Inu anthu anga, mudzachoka ku Babiloni mokondwa, adzakutulutsani mumzindamo mwamtendere. Inu mukufika, mapiri ndi magomo adzakuimbirani nyimbo. Nayonso mitengo yonse yam'thengo idzakuwomberani m'manja.
Ngakhale mikuyu ipande kuchita maluŵa, mipesa ipande kukhala ndi mphesa, mitengo ya olivi ipande kubala zipatso, m'minda musatuluke kanthu, ndipo nkhosa ndi ng'ombe zithe m'khola,
komabe kwanga nkukondwerera mwa Chauta, kwanga nkusangalala chifukwa cha Mulungu Mpulumutsi wanga.
Ambuye anga, Chauta, ndiwo amandipatsa mphamvu. Amalimbitsa miyendo yanga kuti ikhale ngati ya mbaŵala, kuti ndikafike mpaka pamwamba pa phiri. Kwa Woimbitsa nyimbo. Aimbire zazingwe.
Chikondi chosasinthika cha Chauta sichitha, chifundo chakenso nchosatha.
M'maŵa mulimonse zachifundozo zimaoneka zatsopano, chifukwa Chauta ndi wokhulupirika kwambiri.
Imbirani Chauta, inu anthu a dziko lonse lapansi. Lengezani tsiku ndi tsiku za m'mene Iye adapulumutsira anthu ake.
Lalikani za ulemerero wake kwa anthu a mitundu yonse, simbani za ntchito zake zodabwitsa kwa anthu a m'maiko onse.
Chauta ngwamkulu, ngwoyenera kumtamanda kwambiri, ngwoyenera kumuwopa kupambana milungu yonse.
Nchifukwa chake Davide adatamanda Chauta pamaso pa msonkhano wonse. Adati, “Mutamandike mpaka muyaya Inu Chauta, Mulungu wa Israele, kholo lathu.
Inu Ambuye, ndinu aakulu, amphamvu, aulemerero, opambana pa nkhondo ndiponso oposa pa ulemu, pakuti zonse zakumwamba ndi za pansi pano nzanu. Mfumu ndinu nokha, Inu Chauta, ndipo wolamulira zonse ndinu.
Chuma ndi ulemu zimachokera kwa Inu ndipo mumalamulira zonse, chifukwa muli ndi mphamvu zonse. Inu nokha mutha kukweza munthu ndi kumpatsa mphamvu.
Tsopano tikukuthokozani, Inu Mulungu wathu, ndi kutamanda dzina lanu laulemerero.
“Inu Chauta, kodi pali mulungu wina wofanafana nanu? Ndani amafanafana ndi Inu, amene muli aulemu chifukwa cha ungwiro wanu? Ndani amafanafana nanu, Inu amene muli oopsa chifukwa cha ntchito zanu zaulemu ndi zodabwitsa?
Ndidzatamanda dzina la Chauta. Tamandani ukulu wake wa Mulungu.
Nanga chifukwa chiyani munthu mmodzi adagonjetsa anthu chikwi chimodzi, ndipo anthu aŵiri adagonjetsa zikwi khumi? Nchifukwa chakuti Chauta, Mulungu wao, waŵasiya, Mulungu wao wamphamvu waŵataya.
Adani ao amadziŵa kuti milungu yao ndi yopanda mphamvu, ndi yosalingana ndi Mulungu wa Aisraele.
Adani ao ndi oipitsitsa ngati Sodomu ndi Gomora, Ali ngati mipesa yobala mphesa zoŵaŵa ndi zaululu,
ndi oipa kwambiri ngati vinyo wosanganiza ndi ululu wa njoka, ululu wopweteka wa mphiri.
Zimenezitu ndazisunga, ndi zobisika m'chikatikati cha mumtima mwanga.
Kulipsira nkwanga, kubwezera zoyenerera nkwanganso, nthaŵi yoti agwe idzakwana. Tsiku la masoka ao layandikira, chiwonongeko chao chikudza mofulumira.
Chauta adzachitira anthu ake zolungama, adzachitira atumiki ake zachifundo, pamene adzaona kuti mphamvu zao zatha, ndipo kuti sipatsala anthu, kaya ndi akapolo kapena mfulu.
Pamenepo Chauta adzafunsa anthu ake kuti, “Nanga milungu yamphamvu yomwe mumaikhulupirira ija ili kuti?
Mudaidyetsa mafuta a nsembe zanu, mudaipatsa vinyo woti imwe. Ibweretu kuti ikuthandizeni, ikutetezeni.
Muwone tsopano kuti Mulungu uja ndine, Ine ndekha, palibenso mulungu wina. Ndimapha, Ine ndemwe ndimapatsanso moyo, ndimapweteka, Ine ndemwe ndimachiritsanso, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene angathe kupulumutsa munthu m'manja mwanga.
Chauta ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama, ndi Mulungu wokhulupirika ndi wosaipa konse, wachilungamo ndi wosalakwa.