Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

117 Mau a Mulungu Opempherera Mzinda

Ndikakupemphererani mzinda wathu, sindikupempherera malo okha basi, koma anthu onse okhalamo, kuti mtendere ukhale m'nyumba iliyonse, chifukwa mtendere ukufunika kwambiri kuno ku dziko lathu la Malawi komanso padziko lonse lapansi. Monga mmene lemba la Yeremiya 29:7 limatiuza, ndikofunikira 'kufunafuna mtendere wa mzinda umene ndinakutumizani, ndi kuwupempherera kwa Yehova; pakuti m'mtendere wake mudzakhala ndi mtendere inunso'.

Monga ana a Mulungu, ndi udindo wathu kupempherera malo amene tilimo. Tiyenera kulirira ndi kupembedzera mzinda wathu; sitili pano mwangozi, koma kuti tikhale yankho la Mulungu pakati pa mavuto ambiri a anthu okhala m'derali. Ndikukhulupirira kuti aliyense wa ife ali ndi cholinga chofunika m'mzinda momwe timakhala, tilole Mulungu kuti atithandize ngati zida m'manja mwake kuti ambiri amuone kudzera mwa ife.

Tipempherere ana, achinyamata, akuluakulu, ndi okalamba, tilirire kwa Atate kuti chifuniro chake chabwino chichitike m'miyoyo yawo ndi kuti apeze chipulumutso cha miyoyo yawo. Tisalole choipa kulamulira malo amene tilimo, tiyimirire molimba mtima motsutsana ndi mizimu yoipa yomwe ikufuna kulamulira mzinda wathu; tisachite mantha, Mulungu ali nafe ndipo amatipatsa mphamvu zomenyera nkhondo ndi kulengeza ufulu umene Khristu Yesu anatipatsa kudzera mu nsembe yake pa mtanda.

Kumbukirani kuti nkhondo yathu si yolimbana ndi anthu, koma ndi mizimu yoipa ya dziko lino. Tivale zida zonse za Mulungu ndi kukhulupirira kuti tapambana kale. Titsuke manja athu, tikweze mawu athu, ndi kulira kuti Mulungu atichitire chifundo ndi kuti chifuniro chake chichitike monga momwe adakonzerera kuyambira chilengedwe cha dziko lapansi.

Tigwirizane ndi ena, tigwirizane ndi mipingo ina, tisale kudya, tikhale maso usiku, tilowe m'misewu ya mzinda, ndi kulengeza madalitso a Mulungu m'dzina la Yesu.


Miyambo 29:4

Mfumu imalimbitsa dziko pakuweruza molungama, koma imene imaumiriza anthu kuti aipatse ziphuphu, imaononga dziko.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mbiri 7:14

ndipo anthu anga amene amatchedwa dzina langa akadzichepetsa, napemphera, ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zao zoipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwambako. Choncho ndidzaŵakhululukira zoipa zao ndi kupulumutsa dziko lao.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 10:34-35

Petro adayamba kulankhula, adati, “Zoonadi ndazindikira tsopano kuti Mulungu alibe tsankho.

Amalandira bwino munthu wa mtundu uliwonse womuwopa nkumachita chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 122:6-7

Pemphererani mtendere wa Yerusalemu ponena kuti, “Anthu amene amakukonda iwe Yerusalemu, zinthu ziziŵayendera bwino.

Mtendere ukhale m'kati mwa makoma ako, bata likhale m'nyumba zako zachifumu.”

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 2:1-2

Tsono choyamba ndikukupemphani kuti pakhale mapemphero opempherera anthu onse. Mapemphero ake akhale opemba, opempha ndi othokoza Mulungu.

Kwenikweni adzikongoletse ndi ntchito zabwino, monga ayenera kuchitira akazi amene amati ndi opembedza Mulungu.

Akazi pophunzitsidwa, azikhala chete ndi a mtima wodzichepetsa.

Sindilola kuti mkazi aziphunzitsa kapena kukhala ndi ulamuliro pa amuna. Mkazi kwake nkukhala chete.

Paja Adamu ndiye adaayambira kulengedwa, pambuyo pake Heva.

Ndiponso si Adamu amene adaanyengedwa, koma mkaziyo ndiye adaanyengedwa, naphwanya lamulo la Mulungu.

Koma mkazi adzapulumukabe kudzera m'kubala ana, malinga akalimbikira modzichepetsa m'chikhulupiriro, m'chikondi ndi m'kuyera mtima.

Muziŵapempherera mafumu ndi onse amene ali ndi ulamuliro, kuti tikhale ndi moyo wabata ndi wamtendere, tizitamanda Mulungu pa zonse ndi kumadzilemekeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 46:1

Mulungu ndiye kothaŵira kwathu, ndiye mphamvu zathu. Ali wokonzekeratu kutithandiza pa nthaŵi yamavuto.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 26:1-2

Tsiku limenelo m'dziko la Yuda anthu adzaimba nyimbo iyi yakuti, “Tili ndi mzinda wamphamvu, Mulungu amautchinjiriza ndi zipupa ndi malinga.

Munthu woipa mukamchitira zabwino, saphunzira zachilungamo. Amachita zoipa m'dziko lachilungamoli, ndipo amalephera kuzindikira ukulu wa Chauta.

Inu Chauta, mwasamula dzanja lanu kuti muŵalange, koma iwo sakuliwona. Anthuwo achite manyazi poona m'mene mumakondera anthu anu, ndipo moto umene mwasonkhera adani anu, uŵapsereze.

Inu Chauta, mumatipatsa mtendere, chifukwa choti zonse zimene timakhoza, mumatichitira ndinu.

Chauta, Mulungu wathu, ife ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena, sitilemekeza dzina lina, koma lanu lokha.

Ankhanza aja tsopano adafa, sadzakhalanso ndi moyo, sadzabweranso kudzativutitsa, pakuti mwaŵalanga ndi kuŵaonongeratu. Palibenso amene amaŵakumbukira.

Koma Inu Chauta, mwachulukitsa mtundu wathu, mwaukulitsa ndithu. Mwakuza dziko lathu, mwalandirapo ulemu mbali zake zonse.

Inu Chauta, pamene anali m'masautso, anthu anu adakufunafunani, pamene munkaŵalanga, adapemphera kwa Inu.

Inu Chauta, mwatiliritsa monga momwe amalirira mkazi pa nthaŵi yobala mwana.

Ife tidamva ululu, ndipo tidavutika ngati mkazi pa nthaŵi yobala mwana, koma sitidapindule kanthu. Sitidadzetse chipulumutso m'dziko lapansi pano, sitidabadwitse anthu atsopano pansi pano.

Anthu anu amene adafa adzakhalanso ndi moyo, matupi ao adzauka. Inu nonse amene muli m'manda, dzukani ndi kuimba mosangalala. Monga momwe mame amafeŵetsera pansi kutsitsimutsa zomera, momwemonso Chauta adzaukitsa anthu amene adafa kale.

Tsekulani zipata za mzinda, kuti mtundu wotsata malamulo ndi wokhulupirika uloŵe.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:14

“Inu ndinu kuŵala kounikira anthu onse. Mudzi wokhala pamwamba pa phiri sungabisike.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 48:1-2

Chauta ndi wamkulu, ndi woyenera kumutamanda kwambiri. Timuyamike mu mzinda wake, pa phiri lake loyera,

Inu Mulungu, anthu amakutamandani ponseponse, monga dzina lanu latchuka pa dziko lonse lapansi. Dzanja lanu lamphamvu limapambana nthaŵi zonse.

Anthu okhala mu Ziyoni akondwe. A ku Yuda asangalale chifukwa cha kaweruzidwe kanu kolungama.

Zungulirani Ziyoni yense, inde zungulirani mzinda wonsewo, ndipo muŵerenge nsanja zake.

Yang'anani bwino machemba ake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzathe kusimbira mbadwo wakutsogolo.

Mudzati, “Mulungu wathu ndi wotere, ndi Mulungu wathu kuyambira muyaya mpaka muyaya. Iye adzakhala wotitsogolera nthaŵi zonse.”

mzinda wokongola wa Ziyoni pa phiri la Mulungu, wopatsa chimwemwe ku dziko lonse lapansi. Mzinda wa Ziyoni umene uli kumpotowu, ndi mzinda wa Mfumu yathu yaikulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 54:10

Mapiri angathe kusuntha, magomo angathe kugwedezeka, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Lonjezo langa losunga mtendere mpaka muyaya silidzatha,” akuterotu Chauta amene amakumvera chifundo.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 47:12

Pambali pa mtsinjewo, pa gombe lililonse, padzakhala mitengo yobereka zipatso za mtundu uliwonse. Masamba ake sadzafota, ndipo zipatso zake zidzakhala zosalekeza. Izidzabereka mwezi uliwonse, chifukwa madzi ake ndi ochokera ku Nyumba ya Mulungu. Zipatso zake anthu azidzadya, ndipo masamba ake azidzachita mankhwala.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 127:1

Chauta akapanda kumanga nawo nyumba, omanga nyumbayo angogwira ntchito pachabe. Chauta akapanda kulonda nawo mzinda, mlonda angochezera pachabe.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:18

Ngati nkotheka, khalani ndi mtendere ndi anthu onse, monga momwe mungathere.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 29:11

Chauta amapatsa anthu ake mphamvu. Amaŵadalitsa anthu ndi mtendere. Salmo la Davide. Nyimbo yoimba potsekula Nyumba ya Mulungu

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:132

Yang'aneni, ndipo mundikomere mtima monga m'mene mumachitira ndi anthu okukondani.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 19:41-42

Yesu atayandikira, nkuwona Yerusalemu, adalira chifukwa cha mzindawo.

Adati, “Ha, iwenso ukadangodziŵa lero lino zinthu zopatsa mtendere! Koma ai, tsopano maso ako sangathe kuziwona.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 58:12

Anthu anu adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthaŵi yaitali. Adzamanganso pa maziko akalekale. Apo mudzatchedwa anthu okonza makoma, omanganso nyumba zamabwinja, kuti anthu azikhalamo.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:34

Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 115:14

Chauta akudalitseni inu, pamodzi ndi zidzukulu zanu zomwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 122:1

Ndidasangalala pamene adandiwuza kuti, “Tiyeni tipite ku Nyumba ya Chauta.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 33:6

“Komabe m'tsogolo mwake ndidzaupatsanso moyo ndi kuuchiritsa. Anthu ake ndidzaŵachiritsa ndi kuŵapatsa zabwino zochuluka ndi mtendere weniweni.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:9

Ngodala anthu odzetsa mtendere, pakuti Mulungu adzaŵatcha ana ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 1:1-3

Ngwodala munthu wosatsata uphungu wa anthu oipa, wosatsanzira mayendedwe a anthu ochimwa, wosakhala nawo m'gulu la anthu onyoza Mulungu,

koma wokondwerera kumvera malamulo a Chauta, nkumasinkhasinkha za malamulowo usana ndi usiku.

Munthuyo ali ngati mtengo wobzalidwa m'mbali mwa mtsinje wa madzi, ngati mtengo wobereka zipatso pa nthaŵi yake, umene masamba ake safota konse. Zochita zake zonse zimamuyendera bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:36-37

Muphunzitse mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.

Letsani maso anga kuti asamayang'ane zachabe, mundipatse moyo monga momwe mudalonjezera.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:25

Chauta amapasula nyumba ya munthu wonyada, koma amasamalira kadziko ka mkazi wamasiye.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:6-7

Musade nkhaŵa ndi kanthu kalikonse, koma m'mapemphero anu onse muzipempha Mulungu zimene zikusoŵani, ndipo nthaŵi zonse muzipemphe ndi mtima woyamika.

Pamenepo mtendere wochokera kwa Mulungu, umene uli wopitirira nzeru zonse za anthu, udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:3

Khulupirira Chauta ndipo uzichita zabwino. Khala m'dziko ndi kutsata zokhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:4-5

Mundidziŵitse njira zanu, Inu Chauta, mundiphunzitse kuchita kufuna kwanu.

Munditsogolere m'choona chanu ndi kundilangiza, pakuti Inu ndinu Mulungu Mpulumutsi wanga, ndimadalira Inu masiku onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 1:26

Aweruzi ako ndidzaŵakhazikitsanso ngati pa masiku akale aja. Aphungu akonso ndidzaŵakhazikitsanso ngati poyamba paja. Pambuyo pake iweyo udzatchedwa mzinda waungwiro, mzinda wokhulupirika.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:10-11

Sindidabise mumtima mwanga zoti ndinu wolungama. Ndalankhula za kukhulupirika kwanu ndi za chipulumutso chanu. Sindidaŵabisire a pa msonkhano waukulu za chikondi chanu chosasinthika ndi za kukhulupirika kwanu.

Musandichotsere chifundo chanu, Inu Chauta, chikondi chanu chosasinthika ndi kukhulupirika kwanu zindisunge nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 135:21

Atamandike ku Ziyoni Chauta, amene amakhala ku Yerusalemu! Tamandani Chauta!

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:18

Chitani zonse mopemphera, ndi kupempha chithandizo cha Mulungu nthaŵi zonse. Nthaŵi iliyonse muzipemphera motsogoleredwa ndi Mzimu Woyera. Nchifukwa chake muchezere kupemphera mosalekeza, kupempherera anthu onse a Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:14

Amadzetsa mtendere m'malire a dziko lako, amakudyetsa pokupatsa ufa wa tirigu wosalala.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:14-15

Ndipo timalimba mtima pamaso pa Mulungu, popeza kuti amatimvera tikapempha kanthu kalikonse komukomera.

Ndipo ngati tikudziŵa kuti amatimvera tikapempha kanthu kalikonse, timadziŵanso kuti talandiradi zimene tampempha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 9:6-7

Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife. Ulamuliro udzakhala m'manja mwake, ndipo adzamtchula dzina lake lakuti “Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, Mfumu ya Mtendere.”

Ulamuliro ndi mtendere wake zidzanka zikukulirakulira. Iye adzakhala pa mpando wa mfumu Davide, ndipo adzakhazikitsa ndi kuchirikiza ufumu wake, pochita zachilungamo ndi zangwiro kuyambira nthaŵi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse Chauta Wamphamvuzonse watsimikiza kuti adzachitadi zimenezi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:28

Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu, chilungamo ndiye chimalimbitsa ufumu wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 122:9

Chifukwa cha Nyumba ya Chauta, Mulungu wathu, ndidzakupemphera zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:13

Mulungu amene amatipatsa chikhulupiriro, adzaze mitima yanu ndi chimwemwe ndi mtendere pakumvera Iye, kuti chiyembekezo chanu chizikulirakulira ndi mphamvu za Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 121:1-2

Ndimakweza maso anga ku mapiri. Kodi chithandizo changa chimachokera kuti?

Chithandizo changa nchochokera kwa Chauta, amene adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 60:1-3

Iwe Yerusalemu dzuka, ŵala, kuŵala kwako kwayamba. Ulemerero wa Chauta wakuŵalira.

Chauta akuuza Yerusalemu kuti, “Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu ao adzakutumikira. Ndidakulanga pamene ndinali wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndi kukuchitira chifundo.

Zipata zako zidzakhala zotsekula nthaŵi zonse. Usana ndi usiku womwe sadzazitseka, kuti choncho anthu a mitundu yonse adzabwere ndi chuma chao kwa iwe, akuyenda pa mdipiti, mafumu ao ali patsogolo.

Koma maiko ndi mafumu amene sakutumikira, adzaonongekeratu. Anthu a mitundu imeneyo adzaonongeka kotheratu.”

“Mitundu itatu ija ya mitengo ya paini, imene ili yabwino kwambiri m'nkhalango ya ku Lebanoni, adzabwera nayo kuti akongoletsere Nyumba yanga. Motero m'Nyumba m'mene ndimakhala Ine mudzalemekezeka.

Ana a amene adaakuzunzapo adzabwera ndipo adzakugwadira kuwonetsa ulemu. Onse amene adaakunyozapo adzakuŵeramira mpaka pansi. Adzakutchula kuti Mzinda wa Chauta, ndiye kuti Ziyoni, mzinda wa Woyera uja wa Israele.”

“Ngakhale anthu adakusiya nadana nawe, osadutsanso mwa iwe, ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe pa mibadwo ndi mibadwo.

Monga mwana woyamwa udzadya chuma cha anthu a mitundu ina, ndipo mafumu ao omwe adzakusamala. Motero udzadziŵa kuti Ine Chauta ndine Mpulumutsi wako, ndipo kuti ndine Momboli wako, Wamphamvu uja wa Yakobe.”

“Ndidzakupatsa golide m'malo mwa mkuŵa, m'malo mwa chitsulo ndidzakupatsa siliva, mkuŵa m'malo mwa mtengo, chitsulo m'malo mwa mwala. Okuyang'anira ndidzaŵasandutsa amtendere, okulamulira ndidzaŵasandutsa olungama.

Ziwawa sizidzamvekanso. Dziko lako silidzaonongekanso. Ndidzakhala ngati linga lokuteteza, ndipo udzanditamanda chifukwa chokupulumutsa.”

“Sipadzafikanso dzuŵa loti likuŵalire masana, kapena mwezi wokuŵalira usiku. Koma Ine Chauta ndiye ndidzakuŵalire mpaka muyaya. Ine Mulungu wako ndiye ndidzakhale ulemerero wako.

Mdima udzaphimba dziko lapansi, mdima wandiweyani udzagwa pa anthu a mitundu ina. Koma iwe, Chauta adzakuŵalira, ulemerero wake udzaoneka pa iwe.

Chokuunikira ngati dzuŵa sichidzaloŵanso, ndipo chokuunikira ngati mwezi sichidzazimiriranso, chifukwa ndi Chauta amene adzakhala kuŵala kwako mpaka muyaya. Choncho masiku ako olira adzatha.

Anthu ako onse adzayenda m'njira zoyenera, ndipo dzikolo lidzakhala lao mpaka muyaya. Anthuwo ndidaŵaika ndine, ndidaŵalenga ndine, kuti aonetse ulemerero wanga kwa onse.

Ngakhale kabanja kakang'onong'ono kadzasanduka fuko, ndipo kafuko kakang'onong'ono kadzasanduka mtundu wamphamvu. Ndidzachita zimenezi mofulumira nthaŵi yake itafika. Ine ndine Chauta.”

Anthu a mitundu ina adzatsata kuŵala kwako, mafumu adzalondola kunyezimira kwako konga dzuŵa limene likutuluka kumene.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:9

Chauta ndi wabwino kwa onse, amachitira chifundo zamoyo zonse zimene adazilenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:25

Tipulumutseni, tikukupemphani Inu Chauta. Chauta, tikukupemphani kuti zinthu zitiyendere bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:11-12

Uŵapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe. Uŵalanditse amene akuyenda movutikira popita kukaŵapha.

Ukanena kuti, “Ife sitidazidziŵe zimenezi,” kodi iye amene amayesa mtima, zimenezi saziwona? Kodi amene amayang'anira moyo wako sazidziŵa? Kodi sadzambwezera munthu potsata ntchito zake?

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 28:20

Muzikaŵaphunzitsa kusunga zonse zimene Ine ndidakulamulani. Ndipo Ineyo ndili nanu masiku onse, mpaka kutha kwa dziko lino lapansi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:17

Chilichonse chimene mungachite, kaya nkulankhula, kaya nkugwira ntchito, muchichite m'dzina la Ambuye Yesu ndi kuthokoza Mulungu Atate kudzera mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:12

Paja Ambuye amaŵayang'anira bwino anthu olungama amatchera khutu ku mapemphero ao. Koma ochita zoipa saŵayang'ana bwino.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 54:4

Komatu, Mulungu ndiye amandithandiza, Ambuye ndiwo amachirikiza moyo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:31

Nanga tsono tinganenenso chiyani pa zonsezi? Ngati Mulungu ali pa mbali yathu, angatsutsane nafe ndani?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 128:5

Chauta amene amakhala ku Ziyoni akudalitse. Uwone m'mene Yerusalemu zinthu zidzamuyendere bwino masiku onse a moyo wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 32:17

“Ha! Inu Chauta! Mudalenga ndinu dziko lakumwamba ndi dziko lapansi. Mudazilenga ndi dzanja lanu lamphamvu kwambiri. Palibe chokukanikani.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:31

Koma amene amakhulupirira Chauta adzalandira mphamvu zatsopano, adzauluka ngati ziwombankhanga. Adzathamanga koma osatopa, adzayenda koma osalefuka konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 61:1-2

Inu Mulungu, imvani kulira kwanga, mverani pemphero langa.

Ine wokhala ku mathero a dziko lapansi, ndataya mtima, ndipo ndikuitana Inu. Munditsogolere ku thanthwe lalitali.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:24-25

Tizikumbukirana kuti tilimbikitsane kukondana ndi kuchita ntchito zabwino.

Tisamakhalakhala ku misonkhano yathu, monga adazoloŵera ena, koma ife tizilimbitsana mtima, makamaka poona kuti tsiku la Ambuye likuyandikira.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 36:26-27

Ndidzakupatsani mtima watsopano ndi kuloŵetsa mzimu watsopano mwa inu. Ndidzakuchotserani mtima wanu wouma ngati mwalawo ndi kukupatsani mtima wofeŵa ngati mnofu.

Ndidzaika mzimu wanga mwa inu, ndipo ndidzakutsatitsani malangizo anga, ndi kukusungitsani malamulo anga mosamala kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 146:5-6

Ngwodala munthu amene chithandizo chake chimafumira kwa Mulungu wa Yakobe, munthu amene amakhulupirira Chauta, Mulungu wake.

Chauta adalenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili m'menemo. Amasunga malonjezo ake nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:105

mau anu ndiye nyale ya mapazi anga, ndipo amaunikira njira yanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:10

Ufumu wanu udze. Kufuna kwanu kuchitidwe, monga kumwamba chomwechonso pansi pano.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:10

Mulungu akamadalitsa anthu ake, mzinda wonse umatukuka. Oipa akaonongeka, anthu amafuula mwachimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 8:3-4

Ndikamayang'ana ku thambo lanu limene mudapanga ndi manja anu, ndikamaona mwezi ndi nyenyezi zimene mudazikhazika kumeneko,

ndimadzifunsa kuti, “Kodi munthu nchiyani kuti muzimkumbukira, mwana wa munthu nchiyani kuti muzimsamalira?”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 43:1-2

Koma tsopano Chauta amene adakulenga iwe Yakobe, amene adakuumba iwe Israele, akunena kuti, “Usaope, chifukwa ndidakuwombola, ndidachita kukutchula dzina lako, ndiwe wanga.

Inu Aisraele, ndinu mboni zanga, ndinu atumiki anga amene ndidakusankhulani, kuti mundidziŵe ndi kundikhulupirira, ndipo mumvetse kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipadapangidwepo mulungu wina, ndipo pambuyo panga sipadzakhalanso wina.

Chauta ndi Ineyo, mpulumutsi wanu ndine ndekha.

Ndine amene ndidaneneratu zimenezi, ndipo ndine ndidakupulumutsani. Si mulungu wina wachilendo amene adazichita pakati pa inu. Inu nomwe ndinu mboni zanga, ndikutero Ine Chauta.

Ine ndine Mulungu ndipo ndidzakhalapo nthaŵi zonse. Palibe amene angathe kuthaŵa m'manja mwanga, palibe amene angathe kusintha zochita zanga.”

Chauta, Momboli wanu, Woyera uja wa Israele, akunena kuti, “Ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babiloni, kuti ndikupulumutseni. Ndidzagwetsa zipata za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.

Ine ndine Chauta, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israele. Ine ndekha ndine mfumu yanu.”

Kale lija Chauta adapanga njira pa nyanja, njira pakati pa madzi amphamvu.

Adasonkhanitsa magaleta ndi akavalo, ndiponso gulu lankhondo ndi asirikali amphamvu. Onsewo adagwa osadzukanso, adazimitsidwa ndi kutheratu ngati chingwe cha nyale.

Iyeyo akunena kuti, “Musakumbukire zakale kapena kumaganiziranso zinthu zimene zidachitika kale.

Ndikuchita zinthu zatsopano. Zayamba kale kuwoneka, kodi simukuzipenya? Ndikulambula mseu m'chipululu, ndipo ndikukupatsani mitsinje m'dziko louma.

Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe, pamene ukuwoloka mitsinje, siidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto sudzapsa, malaŵi ake sadzakutentha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:12

Ngwodala mtundu wa anthu amene Mulungu wao ndi Chauta, anthu amene Chauta waŵasankha akeake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 12:26

Chiwalo chimodzi chikamamva kuŵaŵa, ziwalo zonse zimamvanso kuŵaŵa. Chiwalo chimodzi chikamalandira ulemu, ziwalo zonse zimakondwa nao.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:2

Muzithandizana kusenza zokulemetsani, ndipo pakutero mumvere ndithu lamulo la Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:26

Ngwodala amene alikudza m'dzina la Chauta. Tikufunirani madalitso ochokera m'nyumba ya Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:12

Muzikhala okondwa chifukwa cha chiyembekezo chanu. Muzipirira pakati pa masautso, ndipo muzipemphera nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:12-13

Kodi pali munthu woopa Chauta? Munthuyo Chauta adzamphunzitsa njira yoti aitsate.

Munthu ameneyo adzakhaladi pabwino, ana ake adzalandira dziko kuti likhale choloŵa chao.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 54:13

Anthu ako ndidzaŵaphunzitsa ndekha, Ine Chauta, ana ako ndidzaŵadalitsa ndi kuŵapatsa mtendere waukulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:32

Ndidzatsata mokondwa njira ya malamulo anu, mukandiwonjezera nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:11

Pakuti Chauta ndiye dzuŵa ndi chishango, amatichitira chifundo ndi kutipatsa ulemu. Chauta saŵamana zabwino anthu oyenda molungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 3:1

Pansi pano chinthu chilichonse chili ndi nyengo yake ndi nthaŵi yake yomwe adaika Mulungu:

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:19

Mulungu wanga ali ndi chuma chochuluka, ndipo mwa Khristu Yesu adzakupatsani zonse zimene mukusoŵa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 56:3

Pamene ndichita mantha ndimadalira Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:6

Paja Chauta ndiye amapatsa nzeru, Iye ndiye kasupe wa kudziŵa zinthu ndi wa kumvetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:1-2

Munthu amene amakhala m'linga la Wopambanazonse, iye amene amakhala mumthunzi mwa Mphambe,

zoipa sizidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi nyumba yako.

Chauta adzapatsa angelo ake ntchito yoti azikulonda kulikonse kumene upite.

Adzakunyamula m'manja mwao, kuwopa kuti phazi lako lingapweteke ndi mwala.

Udzatha kuponda mkango ndi njoka, zoonadi udzaponda ndi phazi lako msona wa mkango ndiponso chinjoka.

Pakuti amene amandikangamira Ine Mulungu mwachikondi, ndidzampulumutsa. Ndidzamteteza popeza kuti amadziŵa dzina langa.

Akadzandiitana, ndidzamuyankha, ndidzakhala naye pa nthaŵi yamavuto. Ndidzamlanditsa ndi kumlemekeza.

Ndidzampatsa moyo wautali ndi kumpulumutsa.

adzanena kwa Chauta kuti, “Inu ndinu kothaŵira kwanga ndi linga langa, ndinu Mulungu wanga amene ndimakukhulupirirani.”

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:22

Ndipo chilichonse chimene timpempha, amatipatsa, chifukwa timatsata malamulo ake, ndipo timachita zomkondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 112:6-7

Pakuti munthu wochita chilungamo sadzagwedezeka konse, sadzaiŵalika mpaka muyaya.

Saopa akamva zoipa zimene zachitika. Mtima wake ndi wosasinthika, amakhulupirira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 26:3

Inu Chauta, mumapatsa mtendere weniweni kwa amene ali ndi mtima wokhazikika, chifukwa chokhulupirira Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:29

Anthu a Mulungu adzalandira dziko kuti likhale lao, ndipo adzakhala m'menemo mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:16

Tiyeni tsono, tiyandikire mopanda mantha ku mpando wachifumu wa Mulungu wokoma mtima. Kumeneko tidzalandira chifundo, ndipo mwa kukoma mtima kwa Mulungu tidzapeza thandizo pa nthaŵi yake yeniyeni.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:1

Thokozani Chauta chifukwa ngwabwino, ndipo chikondi chake nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 58:9

“Mukamapemphera ndidzakumverani, ndipo mukandiitana ndidzakuyankhani. Mukaleka kuzunza anzanu, mukasiya kulozana chala, mukaleka kunena zoipa za anzanu,

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:17

Iyeyo analipo zinthu zonse pakadalibe, mwa Iye zinthu zonse zimalunzana pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:18

Chauta amakhala pafupi ndi anthu a mtima wosweka, amapulumutsa otaya mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 10:1

Abale, chimene ndimakhumbitsa ndi mtima wanga wonse, ndipo chimene ndimapempha Mulungu, ndi chakuti Aisraele apulumuke.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:24

Khalani amphamvu ndipo mulimbe mtima, inu nonse okhulupirira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 127:5

Ngwodala amene phodo lake nlodzaza ndi mivi yotere. Sadzamchititsa manyazi akamalankhula ndi adani ake pa bwalo lamilandu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 56:11

Ndimadalira Mulungu, sindidzachita mantha konse. Kodi munthu angandichite chiyani?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 97:10

Chauta amakonda anthu odana ndi zoipa. Iye amasunga moyo wa anthu ake oyera mtima. Amaŵapulumutsa kwa anthu oipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:4

Ngodala anthu amene amakhala m'Nyumba mwanu, namaimba nyimbo zotamanda Inu nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 5:20

Tsono ndife akazembe oimirira Khristu, ndipo kudzera mwa ifeyo Mulungu mwini ndiye akulankhula nanu mokudandaulirani. Tikukupemphani m'dzina la Khristu kuti muvomere kuyanjananso ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:7

“Pemphani ndipo adzakupatsani. Funafunani ndipo mudzapeza, gogodani, ndipo adzakutsekulirani.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:16

Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino ai, chifukwa Uthengawo ndi mphamvu ya Mulungu yopulumutsa munthu aliyense wokhulupirira, poyamba Ayuda, pambuyo pake anthu a mitundu ina.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 121:3-4

Sadzalola phazi lako kuti literereke, Iye amene amakusunga sadzaodzera.

Zoonadi, amene amasunga Israele, ndithu sadzaodzera kapena kugona.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 33:22

Pakuti Chauta ndiye muweruzi wathu. Chauta ndiye wotilamula, Chauta ndiye mfumu yathu, ndiye amene adzatipulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:147

Ndimadzuka tambala asanalire, kuti ndipemphe chithandizo. Ndimakhulupirira mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:13

Inu abale, Mulungu adakuitanani kuti mukhale mfulu. Koma chenjerani kuti ufulu wanu umenewu usapatse mpata khalidwe lanu lokonda zoipa. Kwenikweni muzitumikirana mwachikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:12

Samalani mayendedwe anu pakati pa akunja, kuti ngakhale azikusinjirirani kuti ndinu anthu ochita zoipa, komabe aziwona ntchito zanu zabwino. Apo adzalemekeza Mulungu pa tsiku limene Iye adzaŵayendere.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 46:10

“Khalani chete, ndipo mudziŵe kuti ndine Mulungu. Mitundu ya anthu imanditamanda, a m'dziko lapansi amandiyamika.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:11

Madalitso olandira anthu olungama amakweza mzinda, koma pakamwa pa anthu oipa mtima pamapasula mzindawo.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 12:2

Ndidzakusandutsa kholo la mtundu waukulu, ndipo ndidzakudalitsa ndi kukusandutsa wotchuka, kotero kuti udzakhala ngati dalitso kwa anthu ena.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 26:3

Khala kuno ndipo Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakudalitsa chifukwa ndidzapereka maiko onseŵa kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako. Ndidzasunga lumbiro limene ndidachita kwa bambo wako Abrahamu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 142:5

Ndimalirira Inu Chauta, ndimati, “Inu ndinu kothaŵira kwanga, ndinu zanga zonse m'dziko la amoyo.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 29:7

Muzikometsa ku mizinda kumene ndidakupirikitsirani ku ukapoloko, kuti zonse zizikuyenderani bwino. Muzipempherera mizindayo kwa Chauta, chifukwa choti mizindayo ikakhala pa mtendere, inunso mudzakhala pabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:17

Muzilemekeza anthu onse. Muzikonda akhristu anzanu. Khalani anthu oopa Mulungu. Mfumu yaikulu koposa ija muziipatsa ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:1

Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wa madzi m'manja mwa Chauta. Amauwongolera ku zimene Iyeyo akufuna.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 22:28

Pakuti ulamuliro ndi wake wa Chauta, Iye amalamula anthu a mitundu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:14

Kumene kulibe uphungu, anthu amagwa, koma kumene kuli aphungu ambiri, kumakhala mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 12:23

Amakuza mitundu ina ya anthu, koma inanso amaiwononga. Amachulukitsa mafuko, nkuŵamwazanso.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 12:25

Yesu adaadziŵa zimenezi, motero adaŵauza kuti, “Anthu a mu ufumu uliwonse akayamba kuukirana, ufumuwo kutha kwake nkomweko. Ndipo anthu a m'mudzi uliwonse kapena a m'banja lililonse akayamba kuukirana, mudzi wotere kapena banja lotere silingalimbe ai.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 2:10-11

Nchifukwa chake tsono khalani anzeru, inu mafumu. Chenjerani inu amene muli olamula dziko lapansi.

Tumikirani Chauta mwamantha ndi monjenjemera.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:1

Munthu aliyense azimvera akulu olamulira, chifukwa palibe ulamuliro umene sudachokere kwa Mulungu. Ndipo olamulira amene alipo, adaŵaika ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Tito 3:1

Uziŵakumbutsa anthu onse kuti azigonjera akulu oweruza ndi olamulira. Aziŵamvera ndipo azikhala okonzeka kuchita ntchito iliyonse yabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:7

Tsono muzipereka kwa onse zimene zikukhalira iwowo: msonkho kwa okhometsa msonkho, zolipira kwa oyenera kuŵalipira. Muzilemekeza oyenera kuŵalemekeza, ndi kuchitira ulemu oyenera kuŵachitira ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 5:29

Koma Petro ndi atumwi enawo adati, “Tiyenera kumvera Mulungu koposa kumvera anthu.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wathu wakumwamba, tikukutamandani ndi kukudalitsani dzina lanu. Tikukuyamikani chifukwa cha zinthu zonse, zikomo chifukwa cha ubwino wanu ndi chifundo chanu chimene chimatsitsidwanso m'mawa uliwonse. Nthawi zonse chikondi chanu chatisunga amoyo. Atate, tikufuna kuona cholinga chanu chokongola chikuchitika mwa munthu aliyense padziko lapansi. Tikubwera pamaso panu ndi mitima yofuna kukhala nanu pafupi, ndi njala ya chifuniro chanu. Lero, tikukupemphani kuti madalitso anu athunthu, amene sasoweketsa chisoni chilichonse, abvire mzinda wathu. Bvumbulutsani mzinda wathu ndi kukhalapo kwanu, ndipo mtendere wanu wopambana luntha lonse utikwanire tonse. Tikukupemphani kuti mudzitamandise mwa nzika iliyonse, kuyambira yaying'ono mpaka yaikulu. Bwerani mulamulire miyoyo yawo, kutenga maganizo awo ndi makhalidwe awo. Choyamba, tikukupemphani kuti muwatenge iwo, chifukwa motero tidzaona kusintha kwakukulu mumzinda. Tengani maluso awo, sinthani mawu awo, ndi kukhazikitsa ufumu wanu wachilungamo ndi choonadi. Tikukupemphani pakali pano, mukhululukire machimo a mzinda wathu, mukhululukire mphulupulu, mutikhululukire chifukwa cha uchimo wambiri ndi kuipa. Tikudzitsika pamaso panu kuti chifundo chanu ndi chisomo chanu chitifikire. Tikulira nthawi yatsopano kumene munthu aliyense adzavomereza Khristu ngati Mpulumutsi wawo ndi kudzichepetsa pamapazi ake. Zikomo Yesu, chifukwa tikudziwa kuti mumamvera mapemphero athu ndipo tidzaona kudzionetsera kwanu. M'dzina la Yesu, Ameni.