Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

NDIME ZA CHIYEMBEKEZO

Chiyembekezo nchofunika kwambiri pa moyo wanga. Ndilimbikitseni mtima wanu mwa Ambuye, khulupirirani kuti mudzaona maloto anu akuti akwaniritsidwa. Musalole kuti mtima wanu ulefuke, pitirizani kupita patsogolo mpaka mutakwaniritsa zomwe mukufuna. Pitirizanibe kuyesetsa, ndipo perekani zonse zomwe mukufuna m'manja mwa Atate wathu wakumwamba.

Ndili Mkristu, sindiyenera kutaya chiyembekezo choti tidzaona Ambuye wathu maso ndi maso, ndipo chifukwa cha nsembe ya Ambuye Yesu Khristu, ndapulumutsidwa ndi chisomo, ndipo tidzakhala naye kosatha. Chiyembekezo mwa Mulungu chimatimasula ku mantha a mtsogolo ndi kusatsimikizika, khulupirirani nthawi zonse Mulungu, kuti adzakupatsani mphamvu zogonjetsa mavuto aliwonse.

“Pakuti ndidziwa bwino lomwe ndikulingalira za inu,” akutero Yehova, “malingaliro a mtendere, osati a choipa, kuti ndikupatseni inu tsogolo ndi chiyembekezo.” (Yeremiya 29:11)


Nyimbo ya Solomoni 8:6-7

Umatirire mtima wako kuti musaloŵe winanso koma ine ndekha, ndipo sudzakumbatira winanso koma ine ndekha. Paja chikondi nchamphamvu ngati imfa, nsanje njaliwuma ngati manda. Chikondi chimachita kuti laŵilaŵi ngati malaŵi a moto, ndipo nchotentha koopsa.

Ngakhale madzi ochuluka sangachizimitse chikondi, ngakhale madzi a chigumula sangachikokolole. Ngakhale munthu atapereka chuma chonse cha m'nyumba chifukwa chofuna kugula chikondi, adzangonyozeka nazo kotheratu. Alongo a Mkazi

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 1:16

Wokondedwa wanga, nawenso ndiwe wokongola, wokongoladi zedi. Malo athu ogonapo ndi msipu wobiriŵira.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 4:7

Ndiwe wokongola kwabasi, iwe wokondedwa wanga. Ulibe nkachilema komwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 4:9

Iwe mlongo wanga, iwe mkazi wanga, wangoti mtima wangawu kwe! Wanditenga mtima ndi kapenyedwe ka maso ako, ndiponso ndi mphande imodzi ya mkanda wa m'khosi mwako.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 4:10

Iwe mlongo wanga, iwe mkazi wanga, chikondi chako nchosangalatsa. Chikondi chako nchosangalatsa kupambana vinyo, mafuta ako ndi onunkhira bwino kupambana zonunkhira zabwino zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 13:8

Chikondi nchosatha. Uneneri udzatha, kulankhula zilankhulo zosadziŵika kudzalekeka, ndipo nzeru za anthu zidzatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 1:4

Tenge, ndizikutsata, tiye tifulumire. Iwe mfumu yanga, kandiloŵetse m'chipinda mwako. Tizisangalala kwambiri ndi kukondwa limodzi. Chikondi chako tichitamande kupambana vinyo. Akazi onse amakukondera kaone!

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 1:15

Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongola, ndiwe chiphadzuŵa. Maso ako akunga ngati nkhunda. Mkazi

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:22

Wopeza mkazi, wapeza chinthu chabwino, Chauta wamukomera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 4:12

Nkotheka kuti munthu apambane mnzake amene ali yekha, koma pakakhala aŵiri, iwoŵa adzalimbana naye. Chingwe cha nkhosi zitatu sichidukirapo.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 1:2

Undimpsompsone ndi milomo yako, chifukwa chikondi chako nchoposa vinyo kukoma kwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 8:7

Ngakhale madzi ochuluka sangachizimitse chikondi, ngakhale madzi a chigumula sangachikokolole. Ngakhale munthu atapereka chuma chonse cha m'nyumba chifukwa chofuna kugula chikondi, adzangonyozeka nazo kotheratu. Alongo a Mkazi

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 13:4-7

Chikondi ncholeza mtima ndiponso nchofatsa. Chikondi chilibe kaduka, ndipo sichidzitamanda kapena kudzikuza.

Chikondi chilibe matama kapena chipongwe, sichidzikonda, sichikwiya, sichisunga mangaŵa.

Sichikondwerera zosalungama, koma chimakondwerera choona.

Chikondi chimakhululukira zonse, chimakhulupirira nthaŵi zonse, sichitaya mtima, ndipo chimapirira onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:14

Kuwonjezera pa zonsezi muzikhala ndi chikondi, pakuti nchimene chimamanga zonse m'chigwirizano chathunthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 2:16

Wokondedwa wangayo ndi wangadi, ndipo ine ndine wake. Amadyetsa gulu lake la ziŵeto pakati pa akakombo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 13:13

Choncho pakali pano zilipo zinthu zitatuzi: chikhulupiriro, chiyembekezo ndi chikondi. Koma mwa zonsezi chopambana ndi chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 8:6

Umatirire mtima wako kuti musaloŵe winanso koma ine ndekha, ndipo sudzakumbatira winanso koma ine ndekha. Paja chikondi nchamphamvu ngati imfa, nsanje njaliwuma ngati manda. Chikondi chimachita kuti laŵilaŵi ngati malaŵi a moto, ndipo nchotentha koopsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 6:3

Wokondedwa wangayo ine ndine wake, ndipo iyeyo ndi wangawanga. Amadyetsa ziŵeto zake pakati pa akakombo. Mwamuna

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 2:24

Nchifukwa chake mwamuna amasiya atate ndi amai, ndipo amaphatikana ndi mkazi wake, choncho aŵiriwo amakhala thupi limodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 2:5

Mundidyetse mphesa zouma, munditsitsimutse ndi maapulosi, pakuti ndikumva chikondi chodwala nacho.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:19

Inu amuna, muzikonda akazi anu, musamaŵavutitse ai.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:33

Komabe akunenanso za inu, kuti mwamuna aliyense azikonda mkazi wake monga momwe amadzikondera iye mwini, ndiponso kuti mkazi aliyense azilemekeza mwamuna wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:12

Chidani chimautsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 31:11-12

Mtima wa mwamuna wake umamkhulupirira, ndipo mwamunayo sadzasoŵa phindu.

Masiku onse a moyo wake, mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino osati zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:19

Ife timakonda Mulungu chifukwa ndiye adayamba kutikonda.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 3:12

Ambuye akulitsirekulitsire kukondana kwanu, ndiponso chikondi chanu cha pa anthu onse, monga momwe chikondi chathu cha pa inu chikukulirakulira.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 2:2

Muja amakhalira kakombo pakati pa minga, ndi m'mene aliri wokondedwa wanga pakati pa atsikana. Mkazi

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:17

Pamene chikondi chafikira pake penipeni mwa ife ndi apa pakuti moyo wathu pansi pano uli wonga moyo wa Khristu, kotero kuti tingathe kukhala olimba mtima pa tsiku la chiweruzo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:8

Chachikulu nchakuti muzikondana mosafookera, popeza kuti chikondi chimaphimba machimo ochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:18

Munthu amene ali ndi chikondi, alibe mantha, pakuti chikondi changwiro chimatulutsira mantha kunja. Munthu akamachita mantha, ndiye kuti akuwopa chilango, ndipo chikondi sichidafike pake penipeni mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 2:18

Pambuyo pake Chauta adati, “Sibwino kuti munthuyu akhale yekha. Ndipanga mnzake woti azimthandiza.”

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:25-28

Inu amuna, muzikonda akazi anu, monga momwe Khristu adakondera Mpingo, nadzipereka chifukwa cha Mpingowo.

Adachita zimenezi kuti aupatule ukhale wakewake, atauyeretsa pakuutsuka ndi madzi ndiponso ndi mau ake.

Adafuna kuti akauimike pamaso pake uli waulemerero, wopanda banga kapena makwinya, kapena kanthu kena kalikonse kouipitsa, koma uli woyera ndi wangwiro kotheratu.

Momwemonso amuna azikonda akazi ao, monga momwe eniakewo amakondera matupi ao. Amene amakonda mkazi wake, ndiye kuti amadzikonda iye yemwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:12

Lamulo langa ndi lakuti muzikondana monga momwe Ine ndakukonderani.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 2:3

Muja umakhalira mtengo wa apulosi pakati pa mitengo yam'nkhalango, ndi m'mene aliri wokondedwa wanga pakati pa anyamata. Ndinkakondwa kwambiri ndikausa mumthunzi mwake, zipatso zake zinali tseketseketseke m'kamwamu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 29:20

Motero Yakobe adagwira ntchito zaka zisanu ndi ziŵiri kuti akwatire Rakele, ndipo nthaŵi imeneyo idangooneka kwa iye ngati masiku oŵerengeka chabe, chifukwa choti adaamkonda kwambiri mkaziyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:3-4

Khalidwe la kudzipereka ndi kukhulupirika zisakuthaŵe, makhalidwe ameneŵa uziyenda nawo ngati mkanda wam'khosi, uŵalembe mumtima mwako.

Usamakangane ndi munthu popanda chifukwa pamene iyeyo sadakuchite choipa chilichonse.

Usachite naye nsanje munthu wachiwawa, usatsanzireko khalidwe lake lililonse.

Paja Chauta amanyansidwa ndi munthu woipa, koma olungama okha amayanjana nawo.

Chauta amatemberera nyumba ya anthu oipa, koma malo okhalamo anthu abwino amaŵadalitsa.

Anthu onyoza, Iye amaŵanyoza, koma odzichepetsa Iye amaŵakomera mtima.

Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

Choncho udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi pa anthunso.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:25

Inu amuna, muzikonda akazi anu, monga momwe Khristu adakondera Mpingo, nadzipereka chifukwa cha Mpingowo.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 3:4

Ndidangoti iwo aja ntaŵapitirira pang'ono, ndampeza amene mtima wanga umamkonda. Ndidamgwira, osamlola kuti achoke, mpaka nditamloŵetsa m'nyumba ya amai anga, m'chipinda cha amene adandibala.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:4

Kondwa mwa Chauta, ndipo adzakupatsa zimene mtima wako ukukhumba.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 5:18

Uzikhutira ndi mkazi wako, uzikondwa ndi mkazi wa unyamata wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 9:9

Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi amene umamkonda, pa masiku onse a moyo wako wopandapakewu umene Mulungu wakupatsa pansi pano. Ndi zokhazo zimene ungaziyembekeze pa moyo wako ndiponso pa ntchito zako zolemetsa zimene umazigwira pansi pano.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:3-5

Ndimayamika Mulungu wanga nthaŵi zonse ndikamakukumbukirani.

Inunso mukumenya nkhondo yomwe ija imene mudandiwona ine ndikuimenya, yomwenso ndikumenyabe tsopano, monga mukumveramu.

Nthaŵi zonse pamene ndikukupemphererani nonsenu, ndimapemphera mokondwa.

Ndiyeneradi kuthokoza chifukwa mwakhala mukugwirizana nane ndi kundithandiza kufalitsa Uthenga Wabwino, kuchokera tsiku limene mudayamba kukhulupirira mpaka tsopano.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 19:4-6

Yesu adaŵayankha kuti, “Kodi simunaŵerenge kuti Mulungu amene adalenga anthu pa chiyambi, adalenga wina wamwamuna, wina wamkazi?

Ndipo kuti Iye yemweyo adati, ‘Nchifukwa chake mwamuna azisiya atate ake ndi amai ake, nakaphatikizana ndi mkazi wake, ndipo aŵiriwo adzasanduka thupi limodzi.’

Choncho tsopano salinso aŵiri koma thupi limodzi. Tsono zimene Mulungu wazilumukiza pamodzi, munthu asazilekanitse.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:17

Bwenzi lako ndiye amakukonda nthaŵi zonse, ndipo mbale wako adabadwira kuti azikuthandiza pa mavuto.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:13-14

Inu abale, Mulungu adakuitanani kuti mukhale mfulu. Koma chenjerani kuti ufulu wanu umenewu usapatse mpata khalidwe lanu lokonda zoipa. Kwenikweni muzitumikirana mwachikondi.

Paja Malamulo onse a Mulungu amaundidwa mkota pa lamulo limodzi lija lakuti, “Uzikonda mnzako monga momwe umadzikondera iwe wemwe.”

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:10

Ngati munthu akonda mnzake, sangamchite choipa ai. Nchifukwa chake amene amakonda mnzake, wasunga zonse zimene Malamulo a Mulungu akunena.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:18

Ananu, chikondi chathu chisamangokhala cha nkhambakamwa chabe, koma chiziwoneka pa zochita zathu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 85:10

Chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika zidzakumana. Chilungamo ndi mtendere zidzagwirizana.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 7:10

Wokondedwayo ine ndine wake, chilakolako chake chonse chili pa ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 31:10

Kodi mkazi wolemerera angathe kumpeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala ya yamtengowapatali.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:2-3

Muzikhala odzichepetsa, ofatsa ndi opirira nthaŵi zonse. Muzilezerana mtima mwachikondi,

Koma umu si m'mene inu mudaphunzirira za Khristu ai,

ngatitu mudamva za Iyeyo, ngatinso mudaphunzitsidwa za Iye, motsata choona chimene chili mwa Yesu.

Mudaphunzira kuti muleke mayendedwe anu akale, muvule moyo wanu wakale uja umene unkadziwononga ndi zilakolako zake zonyenga.

Mtima wanu, umene uli gwero la maganizo anu, usanduke watsopano.

Ndipo muvale moyo watsopano, umene Mulungu adaulenga, wofanafana naye. Apo mudzakhala olungama ndi oyera mtima kwenikweni.

Tsono lekani kunama. Aliyense azilankhula zoona zokhazokha ndi mkhristu mnzake, pakuti tonse pamodzi mogwirizana ndife ziwalo za thupi la Khristu.

Inde mwina nkupsa mtima, koma musachimwe, ndipo musalole kuti dzuŵa likuloŵereni muli chikwiyire.

Musampatse mpata Satana woti akugwetseni.

Amene ankaba, asabenso, koma makamaka azigwira ntchito kolimba ndi kumachita zolungama ndi manja ake, kuti akhale nkanthu kopatsa osoŵa.

M'kamwa mwanu musatuluke mau aliwonse oipa, koma muzinena mau okhaokha abwino ndi olimbitsa mtima monga kungafunikire, kuti mupindulitse anzanu omva mau anuwo.

ndipo muziyesetsa kusunga umodzi mwa Mzimu Woyera pa kulunzana mu mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 5:16

Milomo yake njosangalatsa kwambiri, munthuyo amanditenga mtima kwabasi. Ameneyutu ndiye wokondedwa wanga, ndiponso bwenzi langa, inu akazi a ku Yerusalemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:32

Ndidzatsata mokondwa njira ya malamulo anu, mukandiwonjezera nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:5-6

Mulungu amene amapatsa anthu mphamvu zoti athe kupirira naŵalimbitsa mtima, akuthandizeni kumvana bwino, motsata chitsanzo cha Khristu Yesu,

akuthandizeni kuti ndi mtima umodzi, nonse pamodzi mulemekeze Mulungu ndi Atate a Ambuye athu Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:22-23

Koma zipatso zimene Mzimu Woyera amabweretsa m'moyo wa munthu ndi izi: Chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, kukhulupirika,

kufatsa ndiponso kudziletsa. Zimenezi palibe lamulo loziletsa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 16:14

Zonse zimene muchita, muzichite mwachikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 143:8

Lolani kuti m'maŵa ndimve za chikondi chanu chosasinthika, chifukwa ndimakhulupirira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiziyendamo, pakuti ndimapereka mtima wanga kwa Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 1:2-3

Undimpsompsone ndi milomo yako, chifukwa chikondi chako nchoposa vinyo kukoma kwake.

Mafuta ako odzola ngonunkhira bwino, dzina lako likundikumbutsa za mafuta otsanyukako. Nchifukwa chaketu, atsikana sangaleke kukukonda.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 22:39

Lachiŵiri lake lofanana nalo ndi ili: Uzikonda mnzako monga momwe umadzikondera iwe wemwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 31:10-12

Kodi mkazi wolemerera angathe kumpeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala ya yamtengowapatali.

Mtima wa mwamuna wake umamkhulupirira, ndipo mwamunayo sadzasoŵa phindu.

Masiku onse a moyo wake, mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino osati zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 5:1-2

Munthu wachikulire usamdzudzule mokalipa, koma umchenjeze monga ngati bambo wako. Amuna achinyamata uzikhalitsana nawo ngati abale ako.

Akhale mai woti anthu amamchitira umboni wakuti amachitadi ntchito zabwino. Akhale woti ankalera ana ake bwino, ankalandira bwino alendo, ankasambitsa mapazi a anthu a Mulungu, ndipo ankathandiza anthu amene anali m'mavuto. Akhalenso mai woti ankadzipereka pa ntchito zonse zabwino.

Koma azimai amasiye a zaka zochepera uzikana kuŵalemba m'gulu limeneli. Pajatu zilakolako zao zikayamba kuŵavutitsa nkuŵalekanitsa ndi Khristu, amangofuna kukwatiwanso.

Pamenepo amapezeka olakwa, chifukwa chosasunga lonjezo lao loyamba.

Kuwonjezera pamenepo, amagwa m'chizoloŵezi cha kungokhala khale, motero amangoyendayenda ku nyumba za anthu. Tsonotu samangokhala khale chabe ai, amachitanso miseche nkumaloŵera za eni, ndi kukhala omalankhula zimene samayenera kulankhula.

Nchifukwa chake nkadakonda kuti azimai amasiye a zaka zochepera azikwatiwanso, abale ana, ndipo azisamala bwino panyumba pao, kuti adani athu asapeze mpata wotisinjirira.

Paja alipo kale azimai amasiye ena amene adapatukapo nkumatsata Satana.

Koma ngati mai wina aliyense wachikhristu ali ndi achibale amene ali azimai amasiye, aziŵasamala iyeyo, osasenzetsa mpingo katundu wakeyo. Motero mpingo udzatha kusamala azimai amasiye opanda oŵathandiza.

Akulu a mpingo otsogolera mpingo bwino, akhale oyenera kuŵalemekeza moŵirikiza, makamaka amene amagwira ntchito yolalika mau a Mulungu ndiponso yophunzitsa.

Paja Malembo akuti, “Usaimange pakamwa ng'ombe imene ikupuntha tirigu.” Penanso akuti, “Wantchito ngwoyenera kulandira malipiro ake.”

Usamamvere mau oneneza mkulu wa mpingo, pokhapokha ngati pali mboni ziŵiri kapena zitatu.

Azimai achikulire uzikhalitsana nawo ngati amai ako, ndipo azimai a zaka zochepa uzikhalitsana nawo ngati alongo ako, m'kuyera mtima kwenikweni.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:7

Inunso amuna, muzikhala moŵamvetsa bwino akazi anu. Muziŵachitira ulemu popeza kuti iwowo ndi mtundu wofookerapo, ndiponso ngolandira nanu pamodzi mphatso ya Mulungu, imene ili moyo wosatha. Muzitero, kuti pasakhale kanthu koletsa mapemphero anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:10

Muzikondana kwenikweni monga abale, ndipo muzichita ngati kupikisana poonetsana ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:7

Inu okondedwa, tizikondana, pakuti chikondi nchochokera kwa Mulungu. Aliyense amene ali ndi chikondi, ndi mwana wa Mulungu, ndipo amadziŵa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:3

Ndimayamika Mulungu wanga nthaŵi zonse ndikamakukumbukirani.

Mutu    |  Mabaibulo
Nyimbo ya Solomoni 2:4

Adanditenga kupita nane ku nyumba yaphwando, mbendera yake yozika pa ine inali chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:4

Ukwati muziwulemekeza nonse, ndipo amuna ndi akazi ao azikhala okhulupirika, pakuti anthu adama ndi achigololo Mulungu adzaŵalanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:2

Nchifukwa chake ndikukupemphani kuti mundikondweretse kwenikweni pakuvomerezana maganizo ndi kukondana chimodzimodzi, kukhala a mtima umodzi ndi a cholinga chimodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 7:3-5

Mwamuna azipereka kwa mkazi wake zomuyenerera zokhudza banja ngati mkazi wake, momwemonso mkazi azipereka kwa mwamuna wake zomuyenerera zokhudza banja ngati mwamuna wake.

Amene akulira, akhale monga ngati sakulira, amene akukondwa, akhale monga ngati sakukondwa, amene akugula zinthu, akhale monga ngati sali nazo zinthuzo.

Ndipo amene akugwiritsa ntchito zinthu zapansipano, zisaŵagwire mtima zinthuzo. Pakuti dziko lino lapansi, monga liliri tsopanomu, likupita.

Ndidakakonda kuti pasakhale zokudetsani nkhaŵa. Munthu wosakwatira amangotekeseka ndi za Ambuye, kuganiza za m'mene angakondweretsere Ambuye.

Koma munthu wokwatira amatekeseka ndi zapansipano, kuganiza za m'mene angakondweretsere mkazi wake.

Motero amagwira njakata. Mkazi wosakwatiwa, kapenanso namwali, amangotekeseka ndi za Ambuye, kuti adzipereke kwa Ambuye m'thupi ndi mumzimu momwe. Koma mkazi wokwatiwa amatekeseka ndi zapansipano, kuganiza za m'mene angakondweretsere mwamuna wake.

Ndikunenatu zimenezi kufuna kuti ndikuthandizeni, osati kuti ndikuletseni ufulu wanu ai. Makamaka ndifuna kuti muzichita zonse moyenera, ndipo kuti muzidzipereka kwathunthu potumikira Ambuye.

Koma ngati wina akuganiza kuti akumlakwira namwali wake amene adamtomera, ndipo ngati namwaliyo unamwali wake ukupitirira, tsono munthuyo nkuganiza kuti ayenera kumkwatira, angathe kuchita zimenezo, si kuchimwa ai.

Komabe ngati wina, mwaufulu wake, popanda womukakamiza, watsimikiza kwenikweni kuti samkwatira namwali adamtomerayo, nayenso wachita bwino.

Ndiye kuti, munthu wokwatira namwali amene adamtomera, akuchita bwino, koma woleka osamkwatira, akuchita bwino koposa.

Mkazi amamangika ndi lamulo la ukwati, nthaŵi yonse pamene mwamuna wake ali moyo. Koma mwamuna wake akamwalira, ali ndi ufulu kukwatiwa ndi mwamuna amene iye afuna, malinga ukwatiwo ukhale wachikhristu.

Mkazi thupi lake si lokhalira iye yekha ai, ndi lokhaliranso ndi mwamuna wake yemwe. Momwemonso mwamuna thupi lake si lokhalira iye yekha ai, ndi lokhaliranso ndi mkazi wake yemwe.

Koma m'mene ndikuganizira ine, adzakhala wokondwa koposa ngati akhala wosakwatiwanso. Ndipo ndikuyesa inenso ndili naye Mzimu wa Mulungu.

Musamakanane, koma pokhapokha mutavomerezana kutero pa kanthaŵi kuti mudzipereke ku mapemphero. Pambuyo pake mukhalenso pamodzi, kuwopa kuti Satana angakuyeseni chifukwa cha kulephera kudzigwira.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:32

Muzikomerana mtima ndi kuchitirana chifundo, ndipo muzikhululukirana monga momwe Mulungu mwa Khristu adakukhululukirani inunso.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Chauta wanga wachilungamo ndi wamuyaya, Ambuye Wamkulukulu, m'dzina la Yesu ndikubwera kwa Inu, Inu nokha ndinu woyenera kutamandidwa ndi kupembedzedwa kwakukulu. Mawu anu amati: "Pakuti Ine ndikudziwa malingaliro amene ndili nawo pa inu, ati Yehova, malingaliro a mtendere, osati a choipa, kuti ndikuperekeni chiyembekezo chimene mukuchiyembekezera." Zikomo chifukwa ndimatha kupumula mwa Inu, wotetezeka komanso wodalirika ngati mkango, ngakhale pakati pa mdima wakuda kwambiri, sindidzaopa chifukwa Inu ndinu kuunika kwanga ndi mphamvu yanga. Ambuye, ndithandizeni kuti ndisaike chiyembekezo changa pa zinthu zina, koma mwa Inu nokha. Ndikukuthokozani chifukwa mwandiyesa woyera mwa chisomo chanu, ndikupemphani kuti mundithandize kuti nthawi zonse ndisunge chiyembekezo cha moyo wosatha mwa kuchisunga ndi kuchiyembekezera mumtima mwanga, kuti ndisunge ndi mantha ndi kunjenjemera chipulumutso chachikulu chimenechi chimene mwandipatsa. Ndithandizeni nthawi zonse kuti ndikhale maso pa zinthu za kumwamba osati za padziko lapansi, chifukwa nzika yanga ili kumwamba. M'dzina la Yesu. Ameni.