Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

66 Mau a Mulungu Pa Nzeru ndi Luntha

Mtima wanga ukukukumbutsa kuti nzeru zimachokera kwa Mulungu. Ngati ukufuna kukhala wanzeru, yandikila Iye.

Kuti tizikonda nzeru, choyamba tiyenera kukonda Atate wathu wakumwamba amene amatipatsa nzeruzo. Tsiku lililonse tipemphere nzeru zimene zimachokera kumwamba, kuti tizitha kusankha zinthu mwanzeru zimene zingatithandize kuyenda panjira yoyenera komanso zimene zingatipatse chimwemwe chenicheni mumtima mwathu.

Nzeru ziyenera kukhala nafe nthawi zonse. Tikatero, sitidzalakwitsa zambiri ndipo tidzayenda molimba mtima, chifukwa munthu wanzeru amatha kupeza njira yopitira patsogolo, bola ngati alola Mulungu kumutsogolera. Ngati wina wa inu akusowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, ndipo adzazipatsidwa, chifukwa Mulungu amapereka mowolowa manja kwa onse, popanda kunyoza aliyense. Koma apemphe ndi chikhulupiriro, wopanda kukayika, chifukwa wokayika ali ngati mafunde a m’nyanja, amene amayendayenda ndi mphepo. (Yakobo 1:5-6)

Tifufuze nzeru za Mulungu ndi chikhulupiriro, ndipo tidzazipeza, ndipo tizikumbukira kuti chiyambi cha nzeru ndicho kuopa Yehova. Opa Mulungu, ndipo Iye adzatsogolera mapazi ako. Usalole kuti maganizo ako kapena zakukhosi kwako zikutsogolere, choka pa zoyipa, mvera mawu a Mulungu, mvere Iye, ndipo udzatchedwa wanzeru padziko lapansi.


Aroma 11:33

Chuma cha Mulungu nchachikulu zedi. Nzeru zake ndi kudziŵa kwake nzozama kwambiri. Ndani angamvetse maweruzidwe ake, ndipo njira zake ndani angazitulukire?

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 23:15

Mwana wanga, mtima wako ukakhala wanzeru, nanenso mtima wanga udzasangalala.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 28:28

Choncho adauza munthu kuti, ‘Kuwopa Ambuye ndiye nzeru zimenezo, kuthaŵa zoipa ndiye luntha limenelo.’ ” Yobe

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:20

Woyenda ndi anthu anzeru nayenso amakhala ndi nzeru, koma woyenda ndi zitsiru adzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 1:25

Pajatu chimene chimaoneka ngati kupusa kwa Mulungu, nchanzeru kupambana nzeru za anthu. Ndipo chimene chimaoneka ngati kufooka kwa Mulungu, nchamphamvu kupambana mphamvu za anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:6

Paja Chauta ndiye amapatsa nzeru, Iye ndiye kasupe wa kudziŵa zinthu ndi wa kumvetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:16

Kupata nzeru kumapambana kupata golide. Kumvetsa zinthu nkwabwino, kumapambana kukhala ndi siliva.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:7

Mau a Chauta ngangwiro, amapatsa munthu moyo watsopano. Umboni wa Chauta ndi wokhulupirika, umaŵapatsa nzeru amene alibe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:33

Kuwopa Chauta kumaphunzitsa nzeru, ndipo ndi kudzichepetsa ndi ulemu, chili patsogolo nkudzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 111:10

Kuwopa Chauta ndiye chiyambi cha nzeru. Wotsata malamulo ake amakhala ndi nzeru zenizeni. Chauta ndi wotamandika mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 10:12

Mau a pakamwa pa munthu wanzeru amakondweretsa, koma pakamwa pa chitsiru mpoononga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:14

Udziŵe kuti nzeru ndi yoteronso mumtima mwako. Ukaipeza, zinthu zidzakuyendera bwino m'tsogolo, ndipo chikhulupiriro chako sichidzakhala chachabe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:1

Munthu wokonda mwambo amakonda kudziŵa zinthu, koma wodana ndi chidzudzulo ngwopusa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:17

Koma nzeru zochokera Kumwamba, poyamba nzangwiro, kuwonjeza apo nzamtendere, zofatsa ndi zomvera bwino. Ndi za chifundo chambiri, ndipo zipatso zake zabwino nzochuluka. Nzeruzo sizikondera kapena kuchita chiphamaso.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:7

Kuwopa Chauta ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru ndiye zimanyoza nzeru ndi malangizo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:13

Ngwodala munthu amene wapeza nzeru, amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 9:10

Kulemekeza Chauta ndiye chiyambi cha nzeru, kudziŵa Woyera uja nkukhala womvetsa bwino zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:7

Chachikulu pa nzeru ndi ichi: Kaya nchiyani chimene ungapate, peza nzeruyo, usalephere kupata khalidwe la kumvetsa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:8

Munthu wa mtima wanzeru adzasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:1

Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa atate ake, koma mwana wopusa amanyoza amai ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:5-6

Uzikhulupirira Chauta ndi mtima wako wonse, usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.

Pa ntchito zako zonse uzivomera kuti kuli Mulungu, choncho njira zako Iye adzazilungamitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 29:3

Wokonda nzeru amasangalatsa atate ake, koma amene amayenda ndi akazi adama amamwaza chuma chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:13

Ndani mwa inu ali wanzeru ndi womvetsa zinthu? Aonetse ndi makhalidwe ake abwino kuti nzeru zimaongoleradi zochita zake zofatsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 90:12

Tsono tiphunzitseni kuŵerenga masiku athu, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 4:5-6

Mayendedwe anu pakati pa anthu akunja azikhala anzeru, ndipo muzichita changu, osataya nthaŵi pachabe.

Nthaŵi zonse mau anu akhale okoma, opindulitsa ena, kuti potero mudziŵe m'mene muyenera kuyankhira munthu aliyense.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:15-16

Samalirani bwino mayendedwe anu. Musayende monga anthu opanda nzeru, koma monga anthu anzeru.

Mukhale achangu, osataya nthaŵi yanu pachabe, pakuti masiku ano ngoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:16

Kukwiya kwa munthu wopusa kumadziŵika msanga, koma munthu wanzeru salabadako za chipongwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:3

Amene amagwira pakamwa pake amasunga moyo wake, koma amene amangolakatika amaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 7:10

Usamafunsa kuti, “Chifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?” Limeneli si funso lanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 1:18

Paja nzeru zambiri zimadzetsa chisoni chambiri, munthu akamaonjezera nzeru, ndiye kuti akuwonjezeranso chisoni.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:24

“Munthu aliyense womva mau angaŵa nkumaŵagwiritsa ntchito, amafanafana ndi munthu wanzeru amene adaamanga nyumba yake pa thanthwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 28:29

Nzeru zimenezi zimachokera kwa Chauta Wamphamvuzonse. Uphungu wake ndi wodabwitsa, nzeru zake nzopambana.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:5

Wina mwa inu akasoŵa nzeru, apemphe kwa Mulungu, ndipo adzalandira, pakuti Mulungu amapereka kwa onse mwaufulu ndi mosatonzera.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:5-6

Usaiŵale mau a pakamwa pangaŵa, usatayane nawo, Ukhale ndi nzeru, ndiponso khalidwe la kumvetsa zinthu.

Usaisiye nzeru, ndipo idzakusunga. Uziikonda, ndipo idzakuteteza.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 7:12

Chitetezo cha nzeru chili ngati chitetezo cha ndalama. Koma kudziŵa zinthu kukuposerapo, chifukwa nzeru zimasunga moyo wa amene ali nazo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:130

Kufotokozera mau anu kumakhala ngati kuŵala, kumapatsa nzeru za kumvetsa kwa anthu opanda nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:13

Mau oona amakondweretsa mfumu, ndipo imamkonda munthu wolankhula chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:13-14

Ngwodala munthu amene wapeza nzeru, amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,

pakuti phindu la nzeru nloposa phindu la siliva, nloposanso ndi phindu la golide lomwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:9

Nchifukwa chake, kuyambira tsiku limene tidamva zimenezi, sitileka kukupemphererani. Timapempha Mulungu kuti akudzazeni ndi nzeru ndi luntha, zimene Mzimu Woyera amapatsa, kuti mumvetse zonse zimene Iye afuna.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:29

Wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma wofulumira kupsa mtima amaonetsa uchitsiru wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 12:12

Inde anthu okalamba ali ndi nzeru, anthu amvulazakale ndi omvetsa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 1:30

Mulungu ndiye adakulunzanitsani ndi Khristu Yesu, ndipo adamsandutsa kuti akhale nzeru yathu. Chifukwa cha Yesu, timapezeka olungama pamaso pa Mulungu. Ndi Yesuyo amene amatisandutsa anthu akeake a Mulungu, ndiye amatipulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:13-18

Ngwodala munthu amene wapeza nzeru, amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,

pakuti phindu la nzeru nloposa phindu la siliva, nloposanso ndi phindu la golide lomwe.

Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali. Palibe chinthu chochilakalaka cholingana ndi nzeruyo.

Ndi nzeru imene imakupatsa moyo wautali. Ndi nzeru imene imakuninkha chuma ndi ulemu.

Nzeru imakudzeretsa m'njira za chisangalalo, nimakuyendetsa mumtendere mokhamokha.

Nzeru ili ngati mtengo woŵapatsa moyo oigwiritsa. Ngodala amene amaikangamira molimbika.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:30

Munthu wabwino amalankhula zanzeru, pakamwa pake pamatuluka zachilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 2:26

Pajatu munthu wokondweretsa Mulungu, Mulunguyo amamsandutsa waluntha, wanzeru ndi wosangalala. Koma wochimwa amampatsa ntchito yokunkha ndi younjika zinthu, kenaka zonsezo nkuzipatsa munthu wokondwetsa Mulungu. Zimenezinso nzopanda phindu, ndipo kuyesa kuzimvetsa nkungodzivuta chabe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:8

Amene amakonda nzeru amadzichitira zabwino mwiniwakeyo. Amene ali womvetsa, zinthu zidzamuyendera bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:10-11

Nzeru zidzaloŵa mumtima mwako, kudziŵa zinthu kudzakusangalatsa.

Kuganiziratu zam'tsogolo kudzakusunga, kumvetsa zinthu kudzakuteteza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:66

Patseni luntha ndi nzeru, chifukwa ndimakhulupirira malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:14

Anzeru amakundika nzeru, koma kubwebwetuka kwa chitsiru kumadzetsa chiwonongeko.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:4-5

Mundidziŵitse njira zanu, Inu Chauta, mundiphunzitse kuchita kufuna kwanu.

Munditsogolere m'choona chanu ndi kundilangiza, pakuti Inu ndinu Mulungu Mpulumutsi wanga, ndimadalira Inu masiku onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:15

Zimene amachita munthu wopusa mwiniwakeyo amaziyesa zolungama, koma munthu wanzeru amamvetsera malangizo a ena.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 11:2

Mzimu wa Chauta udzakhala pa Iye, mzimu wopatsa nzeru ndi kumvetsa, mzimu wopatsa uphungu ndi mphamvu, mzimu wopatsa kudziŵa zinthu ndi kuwopa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:15-17

Samalirani bwino mayendedwe anu. Musayende monga anthu opanda nzeru, koma monga anthu anzeru.

Mukhale achangu, osataya nthaŵi yanu pachabe, pakuti masiku ano ngoipa.

Nchifukwa chake musakhale opusa, koma dziŵani zimene Ambuye afuna kuti muchite.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 2:2-3

Ndikufuna kuti zimenezi ziŵalimbitse mtima, ndipo azilunzana pamodzi m'chikondi, azikhala odzaza ndi nzeru zomvetsa zinthu. Motero adzatha kudziŵa mozama chinsinsi cha Mulungu chonena za Khristu.

Mudafa pamodzi ndi Khristu, ndiye kuti simulamulidwanso ndi miyambo ya dziko lapansi. Tsono bwanji mukuchita ngati kuti moyo wanu ukudalirabe zapansipano? Bwanji mukuŵamvera malamulo onga aŵa akuti,

“Usagwire chakuti”, “Usakhudze chakuti”?

Malamulo ameneŵa ndi zophunzitsa zimenezi ndi za anthu chabe, ndipo zimangokhudza zinthu zimene zimatha, anthu akamazigwiritsa ntchito.

Kwinaku mauwo amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamula anthu zambiri pa za kupembedza, za kudzichepetsa ndi za kuzunza thupi lao. Komabe malamulowo alibe phindu, ndipo sathandiza konse kugonjetsa khalidwe longosangalatsa thupi.

Mwa Iyeyu mudzapeza chuma chonse chobisika, ndiye kuti nzeru ndi luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:7-8

Mau a Chauta ngangwiro, amapatsa munthu moyo watsopano. Umboni wa Chauta ndi wokhulupirika, umaŵapatsa nzeru amene alibe.

Malangizo a Chauta ndi olungama, amasangalatsa mtima. Malamulo a Chauta ndi olungama, amapatsa mtima womvetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:14

Maphunzitso a anthu anzeru ali ngati kasupe wa moyo, amathandiza anthu kuti asakodwe mu msampha wa imfa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:30

Palibe nzeru, palibe kumvetsa zinthu, palibe ngakhale uphungu, zimene zingathe kupambana Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:15

Munthu wochenjera amafuna kuphunzirabe zambiri, amafunitsitsa kudziŵa bwino zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:5

Usaiŵale mau a pakamwa pangaŵa, usatayane nawo, Ukhale ndi nzeru, ndiponso khalidwe la kumvetsa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 51:6

Ndithudi, Inu mumakonda mtima woona, choncho mundiphunzitse nzeru zanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:104

Ndimakhala ndi nzeru za kumvetsa chifukwa cha malamulo anu. Nchifukwa chake ndimadana ndi njira iliyonse yonyenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 22:17-18

Utchere khutu lako, umve mau a anthu anzeru, uike mtima wako pa zophunzitsa zanga, kuti uzidziŵe.

Chidzakhala chokondwetsa ukazisunga, ndi kukhala wokonzeka kumazilankhula pa nthaŵi yake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:5

Munthu wanzeru ndi wamphamvu kupambana munthu wa nyonga zambiri, munthu wophunzira amaposa munthu wamphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Atate wanga wakumwamba, Wokondedwa! Inu nokha ndinu woyenera ulemerero ndi ulemu. Zikomo chifukwa chondisonyeza chikondi chanu chosatha ndi chisamaliro chanu. Zikomo chifukwa chondithandiza ndi kundichirikiza nthawi zonse. Ndikupemphani kuti mundipatse nzeru ndipo ndizifune kuposa golide ndi siliva. Mundithandize kuti ndisachite zinthu monga ine ndikufunira, koma monga momwe inu mukufunira. Mawu anu amati: "Kuopa Yehova ndiko nzeru; ndipo kudziwa Woyera ndiwo luntha." Ambuye, sindikufuna kudzidalira ndekha kapena kutsatira nzeru zanga zokha. Nditsogolereni, khalani kapitawo wa boti langa, mundipatse nzeru, mtima womvetsa, ndi mzimu wofunitsitsa kukonzedwa, kuti ndikupatseni chiwongolero cha moyo wanga, chifukwa ndiko chitsimikizo cha chipambano changa chenicheni. M'dzina la Yesu. Amene.