Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -


105 Mauthenga a Mulungu Ponena za Uchiuta wa Khristu

105 Mauthenga a Mulungu Ponena za Uchiuta wa Khristu

Ndikufuna ndikuuzeni anzanga, nthawi zambiri Yesu ankachita ndi kunena zinthu zomwe Mulungu yekha ndiye anali ndi ufulu wozichita ndi kuzinena. Mungaganizire zimenezo!

Ankanena zinthu zosonyeza kuti iye ndi Mulungu. Zimadabwitsa kwambiri!

Ndipo chofunika kwambiri, anapatsidwa ulamuliro, ulemerero, ndi ufumu kuti anthu onse, mitundu yonse, ndi a ziyankhulo zonse azimutumikira. Ulamuliro wake ndi wosatha, sudzatha, ndipo ufumu wake sudzawonongedwa. Tangoganizirani ulamuliro wosatha!

Bukhu la Danieli 7:13-14 limati: “Ndinaona m’masomphenya anga ausiku, ndipo taonani, munthu wonga mwana wa munthu anabwera ndi mitambo ya kumwamba, ndipo anafika kwa Wakale Masiku, ndipo anam’bweretsa pamaso pake. Ndipo anapatsidwa ulamuliro, ulemerero, ndi ufumu, kuti anthu onse, mitundu yonse, ndi a ziyankhulo zonse azimutumikira. Ulamuliro wake ndiwo ulamuliro wosatha umene sudzatha, ndipo ufumu wake sudzawonongedwa.” Apa, Yesu, monga Mwana wa Munthu, akuwonetsedwa kuti ndiye wolamulira wosatha.

Zimenezi zimandipatsa chiyembekezo chachikulu, ndipo ndikukhulupirira kuti zimakupatsaninso chiyembekezo!




Yohane 8:58

Yesu anati kwa iwo, Indetu, indetu, ndinena kwa inu, asanayambe kukhala Abrahamu ndipo Ine ndilipo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 20:28

Tomasi anayankha nati kwa Iye, Ambuye wanga, ndi Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 2:9

pakuti mwa Iye chikhalira chidzalo cha Umulungu m'thupi,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 14:33

Ndipo iwo amene anali m'ngalawamo anamgwadira, nanena, Zoonadi, ndinu Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:1

Pachiyambi panali Mau, ndipo Mau anali kwa Mulungu, ndipo Mau ndiye Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:6

Ndipo pamene atenganso wobadwa woyamba kulowa naye m'dziko, anena, Ndipo amgwadire Iye angelo onse a Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:14

Ndipo Mau anasandulika thupi, nakhazikika pakati pa ife, ndipo tinaona ulemerero wake, ulemerero wonga wa wobadwa yekha wa Atate, wodzala ndi chisomo ndi choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:38

Koma ngati ndichita, mungakhale simukhulupirira Ine, khulupirirani ntchitozo; kuti mukadziwe ndi kuzindikira kuti Atate ali mwa Ine, ndi Ine mwa Atate.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:2

nati, Ali kuti amene anabadwa mfumu ya Ayuda? Chifukwa tinaona nyenyezi yake kum'mawa, ndipo tinadzera kudzamlambira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:30

Ine ndi Atate ndife amodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 28:9

Ndipo onani, Yesu anakomana nao, nanena, Tikuoneni. Ndipo iwo anadza, namgwira Iye mapazi ake, namgwadira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:9

Yesu ananena naye, Kodi ndili ndi inu nthawi yaikulu yotere, ndipo sunandizindikire, Filipo? Iye amene wandiona Ine waona Atate; unena iwe bwanji, Mutionetsere Atate?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:18

Chifukwa cha ichi Ayuda anaonjeza kufuna kumupha, si chifukwa cha kuswa tsiku la Sabata kokha, komatu amatchanso Mulungu Atate wake wa Iye yekha; nadziyesera wolingana ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:8

Koma ponena za Mwana, ati, Mpando wachifumu wanu, Mulungu, ufikira nthawi za nthawi; ndipo ndodo yachifumu yoongoka ndiyo ndodo ya ufumu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:23

Onani namwali adzaima, nadzabala mwana wamwamuna, ndipo adzamutcha dzina lake, Imanuele. Ndilo losandulika, Mulungu nafe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 28:18

Ndipo Yesu anadza nalankhula nao, nanena, Mphamvu zonse zapatsidwa kwa Ine Kumwamba ndi padziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:35

Ndipo mngelo anayankha, nati kwa iye, Mzimu Woyera adzafika pa iwe, ndi mphamvu ya Wamkulukulu idzakuphimba iwe: chifukwa chakenso Choyeracho chikadzabadwa, chidzatchedwa Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:11

pakuti wakubadwirani inu lero, m'mzinda wa Davide, Mpulumutsi, amene ali Khristu Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:3-4

wakunena za Mwana wake, amene anabadwa, wa mbeu ya Davide, monga mwa thupi, akazitape, osinjirira, akumuda Mulungu, achipongwe, odzitama, amatukutuku, oyamba zoipa, osamvera akulu ao, opanda nzeru, osasunga mapangano, opanda chikondi cha chibadwidwe, opanda chifundo; amene ngakhale adziwa kuweruza kwake kwa Mulungu, kuti iwo amene achita zotere ayenera imfa, azichita iwo okha, ndiponso avomerezana ndi iwo akuzichita. amene anatsimikizidwa ndi mphamvu kuti ndiye Mwana wa Mulungu monga mwa Mzimu wa chiyero, ndi kuuka kwa akufa; ndiye Yesu Khristu Ambuye wathu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 9:5

a iwo ali makolo, ndi kwa iwo anachokera Khristu, monga mwa thupi, ndiye Mulungu wa pamwamba pa zonse wolemekezeka kunthawi zonse. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 4:4

mwa amene mulungu wa nthawi ino ya pansi pano anachititsa khungu maganizo ao a osakhulupirira, kuti chiwalitsiro cha Uthenga Wabwino wa ulemerero wa Khristu, amene ali chithunzithunzi cha Mulungu, chisawawalire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 4:4

koma pokwaniridwa nthawi, Mulungu anatuma Mwana wake, wobadwa ndi mkazi, wobadwa wakumvera lamulo,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:20-21

imene anachititsa mwa Khristu, m'mene anamuukitsa kwa akufa, namkhazikitsa padzanja lake lamanja m'zakumwamba, pamwamba pa ukulu wonse, ndi ulamuliro, ndi mphamvu, ndi ufumu, ndi dzina lililonse lotchedwa, si m'nyengo ino ya pansi pano yokha, komanso mwa iyo ikudza;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:5-7

Mukhale nao mtima m'kati mwanu umene unalinso mwa Khristu Yesu, ameneyo, pokhala nao maonekedwe a Mulungu, sanachiyese cholanda kukhala wofana ndi Mulungu, koma anadzikhuthula yekha, natenga maonekedwe a kapolo, nakhala m'mafanizidwe a anthu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:15

amene ali fanizo la Mulungu wosaonekayo, wobadwa woyamba wa chilengedwe chonse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:19

Pakuti kunamkomera Atate kuti mwa Iye chidzalo chonse chikhalire,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 3:16

Ndipo povomerezeka, chinsinsi cha kuchitira Mulungu ulemu nchachikulu: Iye amene anaonekera m'thupi, anayesedwa wolungama mumzimu, anapenyeka ndi angelo, analalikidwa mwa amitundu, wokhulupiridwa m'dziko lapansi, wolandiridwa mu ulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:1-3

Kale Mulungu analankhula ndi makolo mwa aneneri m'manenedwe ambiri ndi mosiyanasiyana, Ndipo, Inu, Ambuye, pachiyambipo munaika maziko ake a dziko, ndipo miyamba ili ntchito ya manja anu. Iyo idzataika; komatu mukhalitsa; ndipo iyo yonse idzasuka monga malaya; ndi monga chofunda mudzaipinda monga malaya, ndipo idzasanduka; koma Inu ndinu yemweyo, ndipo zaka zanu sizidzatha. Koma za mngelo uti anati nthawi iliyonse, Khala padzanja lamanja langa, Kufikira ndikaika adani ako mpando wa kumapazi ako? Kodi siili yonse mizimu yotumikira, yotumidwa kuti itumikire iwo amene adzalowa chipulumutso? koma pakutha pake pa masiku ano analankhula ndi ife ndi Mwana amene anamuika wolowa nyumba wa zonse, mwa Iyenso analenga maiko ndi am'mwamba omwe; ameneyo, pokhala ali chinyezimiro cha ulemerero wake, ndi chizindikiro chenicheni cha chikhalidwe chake, nanyamula zonse ndi mau a mphamvu yake, m'mene adachita chiyeretso cha zoipa, anakhala padzanja lamanja la Ukulu mu Mwamba,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:14

Popeza tsono tili naye Mkulu wa ansembe wamkulu, wopyoza miyamba, Yesu mwana wa Mulungu, tigwiritsitse chivomerezo chathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:20

Ndipo tidziwa kuti Mwana wa Mulungu wafika, natipatsa ife chidziwitso, kuti tizindikire Woonayo, ndipo tili mwa Woonayo, mwa Mwana wake Yesu Khristu. Iye ndiye Mulungu woona ndi moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 1:8

Ine ndine Alefa ndi Omega, ati Ambuye Mulungu, amene ali, amene adali, ndi amene alinkudza, Wamphamvuyonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 22:13

Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza, Chiyambi ndi Chitsiriziro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:16

Ndipo Simoni Petro anayankha nati, Inu ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu wamoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:51

Mkate wamoyo wotsika Kumwamba Ndine amene. Ngati munthu wina akadyako mkate umene, adzakhala ndi moyo kosatha. Inde, ndipo mkate umene ndidzapatsa Ine, ndiwo thupi langa, ukhale moyo wa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 11:25

Yesu anati kwa iye, Ine ndine kuuka ndi moyo: wokhulupirira Ine, angakhale amwalira, adzakhala ndi moyo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 12:6

Koma ndinena kwa inu, kuti wakuposa Kachisiyo ali pompano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 14:61-62

Koma anakhala chete, osayankha kanthu. Mkulu wa ansembe anamfunsanso, nanena naye, Kodi Iwe ndiwe Khristu, Mwana wake wa Wolemekezeka? Ndipo Yesu anati, Ndine amene; ndipo mudzaona Mwana wa Munthu alikukhala kudzanja lamanja la mphamvu, ndi kudza ndi mitambo ya kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 9:35

Ndipo munatuluka mau mumtambo, nanena, Uyu ndiye Mwana wanga, wosankhidwayo; mverani Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:22

Zonse zaperekedwa kwa Ine ndi Atate wanga; ndipo palibe munthu azindikira Mwana ali yani, koma Atate; ndipo Atate ali yani, koma Mwana, ndi iye amene Mwana afuna kumuululira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 3:16

Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wake wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira Iye asatayike, koma akhale nao moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:22

Pakuti Atate saweruza munthu aliyense, koma anapereka kuweruza konse kwa Mwana;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:6

Yesu ananena naye, Ine ndine njira, ndi choonadi, ndi moyo. Palibe munthu adza kwa Atate, koma mwa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 10:9

kuti ngati udzavomereza m'kamwa mwako Yesu ndiye Ambuye, ndi kukhulupirira mumtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 8:6

koma kwa ife kuli Mulungu mmodzi, Atate amene zinthu zonse zichokera kwa Iye, ndi ife kufikira kwa Iye; ndi Ambuye mmodzi Yesu Khristu, amene zinthu zonse zili mwa Iye, ndi ife mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 12:3

Chifukwa chake ndikuuzani inu, kuti palibe munthu wakulankhula mwa Mzimu wa Mulungu, anena, Yesu ngwotembereredwa; ndipo palibe wina akhoza kunena, Yesu ali Ambuye, koma mwa Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 5:19

ndiko kunena kuti Mulungu anali mwa Khristu, alinkuyanjanitsa dziko lapansi kwa Iye yekha, osawawerengera zolakwa zao; ndipo anaikiza kwa ife mau a chiyanjanitso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:20

Ndinapachikidwa ndi Khristu; koma ndili ndi moyo; wosatinso ine ai, koma Khristu ali ndi moyo mwa ine; koma moyo umene ndili nao tsopano m'thupi, ndili nao m'chikhulupiriro cha Mwana wa Mulungu, amene anandikonda, nadzipereka yekha chifukwa cha ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 3:20-21

Ndipo kwa Iye amene angathe kuchita koposaposatu zonse zimene tizipempha, kapena tiziganiza, monga mwa mphamvu ya kuchita mwa ife, kwa Iye ukhale ulemerero mu Mpingo ndi mwa Khristu Yesu, kufikira mibadwo yonse ya nthawi za nthawi. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:1

Chifukwa chake ngati munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, funani zakumwamba, kumene kuli Khristu wokhala padzanja lamanja la Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:4

amene pakudza kwa Iye, mwala wamoyo, wokanidwatu ndi anthu, koma ndi Mulungu wosankhika, waulemu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:2

(ndipo moyowo unaonekera, ndipo tidaona, ndipo tichita umboni, ndipo tikulalikirani moyo wosathawo, umene unali kwa Atate, nuonekera kwa ife);

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:2

M'menemo muzindikira Mzimu wa Mulungu: mzimu uliwonse umene uvomereza kuti Yesu Khristu anadza m'thupi, uchokera mwa Mulungu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 4:12

Ndipo palibe chipulumutso mwa wina yense, pakuti palibe dzina lina pansi pa thambo la kumwamba, lopatsidwa mwa anthu, limene tiyenera kupulumutsidwa nalo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 16:31

Ndipo iwo anati, Ukhulupirire Ambuye Yesu, ndipo udzapulumuka, iwe ndi apabanja ako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:16

Pakuti Uthenga Wabwino sundichititsa manyazi; pakuti uli mphamvu ya Mulungu yakupulumutsa munthu aliyense wakukhulupirira; kuyambira Myuda, ndiponso Mgriki.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 7:3

wopanda atate wake, wopanda amake, wopanda mawerengedwe a chibadwidwe chake, alibe chiyambi cha masiku ake kapena chitsiriziro cha moyo wake, wofanizidwa ndi Mwana wa Mulungu), iyeyu wakhala wansembe kosalekeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:12

koma Iye, m'mene adapereka nsembe imodzi chifukwa cha machimo, anakhala padzanja lamanja la Mulungu chikhalire;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 2:5

Pakuti pali Mulungu mmodzi, ndi Mtetezi mmodzi pakati pa Mulungu ndi anthu, ndiye munthu, Khristu Yesu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 2:13

akulindira chiyembekezo chodala, ndi maonekedwe a ulemerero wa Mulungu wamkulu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 5:12

akunena ndi mau aakulu, Ayenera Mwanawankhosa, wophedwayo, kulandira chilimbiko, ndi chuma, ndi nzeru, ndi mphamvu, ndi ulemu, ndi ulemerero, ndi chiyamiko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 19:16

Ndipo ali nalo pa chovala chake ndi pa ntchafu yake dzina lolembedwa, MFUMU YA MAFUMU, NDI MBUYE WA AMBUYE.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:11

Ndipo pofika kunyumba anaona kamwanako ndi Maria amake, ndipo anagwa pansi namgwadira Iye; namasula chuma chao, nampatsa Iye mitulo, ndiyo golide ndi lubani ndi mure.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 17:5

Akali chilankhulire, onani, mtambo wowala unawaphimba iwo: ndipo onani, mau ali kunena mumtambo, Uyu ndiye Mwana wanga wokondedwa, mwa iyeyu ndikondwera, mverani Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 28:19

Chifukwa chake mukani, phunzitsani anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza iwo m'dzina la Atate, ndi la Mwana, ndi la Mzimu Woyera:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 1:1

Chiyambi chake cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 9:7

Ndipo panadza mtambo wakuwaphimba iwo; ndipo mau munatuluka m'mtambomo, kuti, Uyu ndiye Mwana wanga wokondedwa; mverani Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 4:41

Ndi ziwanda zomwe zinatuluka mwa ambiri, ndi kufuula, kuti, Inu ndinu Mwana wa Mulungu. Ndipo Iye anazidzudzula, wosazilola kulankhula, chifukwa zinamdziwa kuti Iye ndiye Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 12:41

Izi anati Yesaya, chifukwa anaona ulemerero wake; nalankhula za Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 17:5

Ndipo tsopano, Atate Inu, lemekezani Ine ndi Inu nokha ndi ulemerero umene ndinali nao ndi Inu lisanakhale dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 17:24

Atate, amene mwandipatsa Ine, ndifuna kuti, kumene ndili Ine, iwonso akhale pamodzi ndi Ine; kuti ayang'anire ulemerero wanga, umene mwandipatsa Ine; pakuti munandikonda Ine lisanakhazikike dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:31-32

Ndipo tidzatani ndi zinthu izi? Ngati Mulungu ali ndi ife, adzatikaniza ndani? Iye amene sanatimane Mwana wake wa Iye yekha, koma anampereka chifukwa cha ife tonse, adzalekeranji kutipatsanso ife zinthu zonse kwaulere pamodzi ndi Iye?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 13:14

Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu, ndi chikondi cha Mulungu, ndi chiyanjano cha Mzimu Woyera zikhale ndi inu nonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 1:3

Chisomo kwa inu, ndi mtendere wa kwa Mulungu Atate, ndi Ambuye wathu Yesu Khristu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:18

kuti mwa Iye ife tonse awiri tili nao malowedwe athu kwa Atate, mwa Mzimu mmodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:19

Koma Mulungu wanga adzakwaniritsa chosowa chanu chilichonse monga mwa chuma chake mu ulemerero mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:27

kwa iwo amene Mulungu anafuna kuwazindikiritsa ichi chimene chili chuma cha ulemerero wa chinsinsi pakati pa amitundu, ndiye Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 2:3

amene zolemera zonse za nzeru ndi chidziwitso zibisika mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 1:10

ndi kulindirira Mwana wake achokere Kumwamba, amene anamuukitsa kwa akufa, Yesu, wotipulumutsa ife kumkwiyo ulinkudza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 1:1

Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu monga mwa chilamuliro cha Mulungu Mpulumutsi wathu, ndi cha Khristu Yesu, chiyembekezo chathu:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 1:4

kwa Tito, mwana wanga weniweni monga mwa chikhulupiriro cha ife tonse: Chisomo ndi mtendere za kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 3:1

Potero, abale oyera mtima, olandirana nao maitanidwe akumwamba, lingirirani za Mtumwi ndi Mkulu wa ansembe wa chivomerezo chathu, Yesu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:6

koma wopanda chikhulupiriro sikutheka kumkondweretsa; pakuti iye wakudza kwa Mulungu ayenera kukhulupirira kuti alipo, ndi kuti ali wobwezera mphotho iwo akumfuna Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:3

Wodalitsika Mulungu ndiye Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Iye amene, monga mwa chifundo chake chachikulu, anatibalanso ku chiyembekezo cha moyo, mwa kuuka kwa akufa kwa Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:23

Yense wakukana Mwana, alibe Atate; wovomereza Mwana ali ndi Atatenso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:11-12

Ndipo uwu ndi umboniwo, kuti Mulungu anatipatsa ife moyo wosatha, ndipo moyo umene uli mwa Mwana wake. Iye wakukhala ndi Mwana ali nao moyo; wosakhala ndi Mwana wa Mulungu alibe moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 1:8

Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ndi mu Yudeya monse, ndi mu Samariya, ndi kufikira malekezero ake a dziko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:36

Pamenepo lizindikiritse ndithu banja lililonse la Israele, kuti Mulungu anamuyesa Ambuye ndi Khristu, Yesu amene inu munampachika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 10:42

Ndipo anatilamulira ife tilalikire kwa anthu, ndipo tichite umboni kuti Uyu ndiye amene aikidwa ndi Mulungu akhale woweruza amoyo ndi akufa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:10

Pakuti ngati, pokhala ife adani ake, tinayanjanitsidwa ndi Mulungu mwa imfa ya Mwana wake, makamaka ndithu, popeza ife tayanjanitsidwa, tidzapulumuka ndi moyo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:23

Pakuti mphotho yake ya uchimo ndi imfa; koma mphatso yaulere ya Mulungu ndiyo moyo wosatha wa mwa Khristu Yesu Ambuye wathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 2:9

koma monga kulembedwa, Zimene diso silinazione, ndi khutu silinazimve, nisizinalowe mu mtima wa munthu, zimene zilizonse Mulungu anakonzereratu iwo akumkonda Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:57

koma ayamikike Mulungu, amene atipatsa ife chigonjetso mwa Ambuye wathu Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 3:26

Pakuti inu nonse muli ana a Mulungu, mwa chikhulupiriro cha mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:7

Tili ndi maomboledwe mwa mwazi wake, chikhululukiro cha zochimwa, monga mwa kulemera kwa chisomo chake,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:3-4

Pakuti munafa, ndipo moyo wanu wabisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu. Pamene Khristu adzaoneka, ndiye moyo wathu, pamenepo inunso mudzaonekera pamodzi ndi Iye mu ulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:14-15

kuti usunge lamulolo, lopanda banga, lopanda chilema, kufikira maonekedwe a Ambuye wathu Yesu Khristu; limene adzalionetsa m'nyengo za Iye yekha, amene ali Mwini Mphamvu wodala ndi wayekha, ndiye Mfumu ya mafumu ndi Mbuye wa ambuye;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:8

Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, ndi lero, ndi kunthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:10

Ndipo Mulungu wa chisomo chonse, amene adakuitanani kulowa ulemerero wake wosatha mwa Khristu, mutamva zowawa kanthawi, adzafikitsa inu opanda chilema mwini wake, adzakhazikitsa, adzalimbikitsa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:1

Taonani, chikondicho Atate watipatsa, kuti titchedwe ana a Mulungu; ndipo tili ife otere. Mwa ichi dziko lapansi silizindikira ife, popeza silimzindikira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:15

Iye amene adzavomereza kuti Yesu ali Mwana wa Mulungu, Mulungu akhala mwa iye, ndi iye mwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 7:10

ndipo afuula ndi mau aakulu, nanena, Chipulumutso kwa Mulungu wathu wakukhala pa mpando wachifumu, ndi kwa Mwanawankhosa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 11:15

Ndipo mngelo wachisanu ndi chiwiri anaomba lipenga, ndipo panakhala mau aakulu mu Mwamba, ndi kunena, Ufumu wa dziko lapansi wayamba kukhala wa Ambuye wathu, ndi wa Khristu wake: ndipo adzachita ufumu kufikira nthawi za nthawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 22:20

Iye wakuchitira umboni izi, anena, Indetu; ndidza msanga. Amen; idzani, Ambuye Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:36

kodi inu munena za Iye, amene Atate anampatula namtuma kudziko lapansi, Uchita mwano; chifukwa ndinati, Ndili Mwana wa Mulungu?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga wachilungamo, ndinu wamkulu komanso wodabwitsa, inu amene mukhala pampando wachifumu mutavala ulemerero ndi mphamvu, inu woposa zonse ndiponso wangwiro pa zonse zimene muchita. Yesu wokondedwa ndikubwerera kwa inu, chifukwa inu nokha muli ndi ulemerero, mphamvu ndi ufumu, ndikupemphani mundidzetse ndi kukhalapo kwanu ndipo Mzimu wanu Woyera uwonekere pa moyo wanga. Ndithandizeni kutsatira chikhulupiriro chanu ndi kumvera kulikonse kumene ndikupita ndipo kukhalapo ndi Mphamvu ya Mzimu wanu Woyera zikhale zooneka pa moyo wa omwe akumva mawu anu mkamwa mwanga. Mawu anu amati: “Pamenepo amene anali m’ngalawa anamulambira Iye, nanena, Zoonadi ndinu Mwana wa Mulungu.” Mundiphunzitse Yesu kuyenda monga momwe munayendera, kuchiritsa odwala, kumasula ogwidwa ndi kuthandiza onse otsenderezedwa. Munandipulumutsa ku mphamvu ya mdima, Yesu ndinu Mwana wa Mulungu, mkhalapakati pakati pa Mulungu ndi munthu, zikomo chifukwa munadzipereka chifukwa cha chikondi cha anthu polipira mtengo wapatali chifukwa cha machimo athu. Zikomo chifukwa chosandisiya konse komanso kundifuna nthawi zonse. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa