Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Akolose 1:19 - Buku Lopatulika

19 Pakuti kunamkomera Atate kuti mwa Iye chidzalo chonse chikhalire,

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

19 Pakuti kunamkomera Atate kuti mwa Iye chidzalo chonse chikhalire,

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

19 Kudakomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristuyo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

19 Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu.

Onani mutuwo Koperani




Akolose 1:19
12 Mawu Ofanana  

Nthawi yomweyo Iye anakondwera ndi Mzimu Woyera, nati, Ndikuvomerezani Inu, Atate, Ambuye wa kumwamba ndi dziko lapansi, kuti izi munazibisira anzeru ndi ozindikira, ndipo munaziululira ana amakanda; indedi, Atate, pakuti kotero kudakondweretsa pamaso panu.


Chifukwa mwa kudzala kwake tinalandira ife tonse, chisomo chosinthana ndi chisomo.


Pakuti Iye amene Mulungu anamtuma alankhula mau a Mulungu; pakuti sapatsa Mzimu ndi muyeso.


Pakuti popeza m'nzeru ya Mulungu dziko lapansi, mwa nzeru yake, silinadziwe Mulungu, chidamkonda Mulungu kupulumutsa okhulupirirawo mwa chopusa cha kulalikira.


amene ali thupi lake, mdzazidwe wa Iye amene adzaza zonse m'zonse.


Wolemekezeka Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene anatidalitsa ife ndi dalitso lonse la mzimu m'zakumwamba mwa Khristu;


Anatikonzeratu tilandiridwe ngati ana a Iye yekha mwa Yesu Khristu, monga umo kunakomera chifuniro chake,


Iye wotsikayo ndiye yemweyonso anakwera, popitiriratu miyamba yonse, kuti akadzaze zinthu zonse.


amene zolemera zonse za nzeru ndi chidziwitso zibisika mwa Iye.


pakuti mwa Iye chikhalira chidzalo cha Umulungu m'thupi,


pamene palibe Mgriki ndi Ayuda, mdulidwe ndi kusadulidwa, watchedwa wakunja, Msukuti, kapolo, mfulu, komatu Khristu ndiye zonse, ndi m'zonse.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa