Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 12:6 - Buku Lopatulika

6 Koma ndinena kwa inu, kuti wakuposa Kachisiyo ali pompano.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Koma ndinena kwa inu, kuti wakuposa Kachisiyo ali pompano.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Ndipotu ndikunenetsa kuti pali wina pano woposa Nyumba ya Mulunguyo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Ine ndikuwuzani kuti wamkulu kuposa Nyumba ya Mulunguyo ali pano.

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 12:6
12 Mawu Ofanana  

Koma kodi nzoona kuti Mulungu akhala ndi anthu padziko lapansi? Taonani, thambo, inde m'mwambamwamba, sizifikira inu, koposa kotani nanga nyumba iyi ndaimanga?


Atero Yehova, Kumwamba ndi mpando wanga wachifumu, ndi dziko lapansi ndi choikapo mapazi anga; mudzandimangira Ine nyumba yotani? Ndi malo ondiyenera kupumamo ali kuti?


Pakuti zonsezi mkono wanga wazilenga, momwemo zonsezi zinaoneka, ati Yehova; koma ndidzayang'anira munthu uyu amene ali waumphawi, ndi wa mzimu wosweka, nanthunthumira ndi mau anga.


Taonani, ndituma mthenga wanga, kuti akonzeretu njira pamaso panga; ndipo Ambuye amene mumfuna adzadza ku Kachisi wake modzidzimutsa; ndiye mthenga wa chipangano amene mukondwera naye; taonani akudza, ati Yehova wa makamu.


Kapena simunawerenge kodi m'chilamulo, kuti tsiku la Sabata ansembe mu Kachisi amaipitsa tsiku la Sabata, nakhala opanda tchimo?


pakuti mwa Iye chikhalira chidzalo cha Umulungu m'thupi,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa