Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


76 Mau a Mulungu Oteteza Ku Zoipa

76 Mau a Mulungu Oteteza Ku Zoipa

Masalmo 68:20 amatiuza kuti Mulungu ndiye chipulumutso chathu, ndiye amene amatitulitsa ku imfa. Ngakhale mtsogolo mulibe chitsimikizo, kusankha mwanzeru kungatipatse moyo wautali.

Miyambo 13:14 imati nzeru ndiye chitsime cha moyo, ndipo imateteza otsatira ake ku misampha ya imfa. Baibulo limalonjeza mtsogolo mopanda imfa, koma pano padziko lapansi, ndikofunika kugwiritsa ntchito mpata umene Mulungu watipatsa, kukhala mogwirizana ndi malamulo ake, kusunga malamulo ake mumtima mwathu, ndikuzisinkhasinkha usana ndi usiku.

Moyo umenewu, woperekedwa ndi Yehova, umatipatsa mwayi wokhala padziko lapansi limene watipatsa, komanso m'nyumba zakumwamba zimene Atate wathu anakonzeratu. Popeza imfa siidziwika nthawi yake, ndikofunikira kukhala moyanjana ndi Mulungu ndi anansi athu, kufunafuna kuyera pamaso pa Ambuye nthawi zonse.

Motero Yehova adzatuma angelo ake kuti atiteteze ku zoopsa zonse, kuti tisapunthwe, chifukwa tamvera mawu ake. Osachita mantha, pakuti Mulungu adzakhala nafe, adzatikhutiritsa nthawi ya chilala, adzalimbitsa mafupa athu, ndi kutiphimba ndi kukhalapo kwake kwamuyaya.




Masalimo 118:18

Kulanga anandilangadi Yehova: koma sanandipereke kuimfa ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Hoseya 13:14

Ndidzawaombola kumphamvu ya kumanda, ndidzawaombola kuimfa; imfa, miliri yako ili kuti? Kulekerera kudzabisika pamaso panga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:28

Indetu ndinena kwa inu, kuti alipo ena a iwo aima pano sadzalawa ndithu imfa, kufikira adzaona Mwana wa Munthu atadza mu ufumu wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:5

Ndi chikhulupiriro Enoki anatengedwa kuti angaone imfa; ndipo sanapezeke, popeza Mulungu adamtenga: pakuti asanamtenge, anachitidwa umboni kuti anakondweretsa Mulungu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 56:13

Pakuti mwalanditsa moyo wanga kuimfa, simunatero nao mapazi anga kuti ndingagwe? Kuti ndiyende pamaso pa Mulungu m'kuunika kwa amoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 121:7-8

Yehova adzakusunga kukuchotsera zoipa zilizonse; adzasunga moyo wako. Yehova adzasungira kutuluka kwako ndi kulowa kwako, kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:11

Tavalani zida zonse za Mulungu, kuti mudzakhoze kuchilimika pokana machenjerero a mdierekezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 28:15

Taonani, Ine ndili pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakusunga iwe konse kumene upitako, ndipo ndidzakubwezanso iwe ku dziko lino; chifukwa kuti sindidzakusiya iwe, kufikira kuti nditachita chimene ndanena nawe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 41:2

Yehova adzamsunga, nadzamsunga ndi moyo, ndipo adzadalitsika padziko lapansi, ndipo musampereke ku chifuniro cha adani ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 68:20

Mulungu akhala kwa ife Mulungu wa chipulumutso; ndipo Yehova Ambuye ali nazo zopulumutsira kuimfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 9:2

Anthu amene anayenda mumdima, aona kuwala kwakukulu; iwo amene anakhala m'dziko la mthunzi wa imfa, kuwala kwatulukira kwa iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:24

Indetu, indetu, ndinena kwa inu, kuti iye wakumva mau anga, ndi kukhulupirira Iye amene anandituma Ine, ali nao moyo wosatha, ndipo salowa m'kuweruza, koma wachokera kuimfa, nalowa m'moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 25:8

Iye wameza imfa kunthawi yonse; ndipo Ambuye Mulungu adzapukuta misozi pa nkhope zonse; ndipo chitonzo cha anthu ake adzachichotsa padziko lonse lapansi; chifukwa Yehova wanena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 91:1-2

Iye amene akhala pansi m'ngaka yake ya Wam'mwambamwamba adzagonera mu mthunzi wa Wamphamvuyonse. palibe choipa chidzakugwera, ndipo cholanga sichidzayandikiza hema wako. Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, akusunge m'njira zako zonse. Adzakunyamula pa manja ao, ungagunde phazi lako pamwala. Udzaponda mkango ndi mphiri; udzapondereza msona wa mkango ndi chinjoka. Popeza andikondadi ndidzampulumutsa; ndidzamkweza m'mwamba, popeza adziwa dzina langa. Adzandifuulira Ine ndipo ndidzamyankha; kunsautso ndidzakhala naye pamodzi; ndidzamlanditsa, ndi kumchitira ulemu. Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri, ndi kumuonetsera chipulumutso changa. Ndidzati kwa Yehova, Pothawirapo panga ndi linga langa; Mulungu wanga, amene ndimkhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 5:11

Chifukwa chake anatumiza, nasonkhanitsa mafumu onse a Afilisti, ndipo iwowa anati, Chotsani likasa la Mulungu wa Israele, lipitenso kumalo kwake, kuti lingationonge ife, ndi anthu athu; pakuti kunali kusautsa koopsa m'mzinda monse; dzanja la Mulungu linavutadi pamenepo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:22

Pakuti monga mwa Adamu onse amwalira, choteronso mwa Khristu onse akhalitsidwa ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 18:32

Pakuti sindikondwera nayo imfa ya wakufayo, ati Ambuye Yehova; chifukwa chake bwererani, nimukhale ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:21

Pakuti monga imfa inadza mwa munthu, kuuka kwa akufa kunadzanso mwa munthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:28

M'khwalala la chilungamo muli moyo; m'njira ya mayendedwe ake mulibe imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 4:16

anthu akukhala mumdima adaona kuwala kwakukulu, ndi kwa iwo okhala m'malo a mthunzi wa imfa, kuwala kunatulukira iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 8:51

Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Munthu akasunga mau anga, sadzaona imfa nthawi yonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:2

Pakuti chilamulo cha mzimu wa moyo mwa Khristu Yesu chandimasula ine ku lamulo la uchimo ndi la imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:12

Chifukwa kuti kulimbana kwathu sitilimbana nao mwazi ndi thupi, komatu nao maukulu, ndi maulamuliro, ndi akuchita zolimbika a dziko lapansi a mdima uno, ndi auzimu a choipa m'zakumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 50:20

Koma inu, munandipangira ine choipa; koma Mulungu anachipangira chabwino, kuti kuchitike monga lero, kupulumutsa amoyo anthu ambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 54:17

Palibe chida chosulidwira iwe chidzapindula; ndipo lilime lonse limene lidzakangana nawe m'chiweruzo udzalitsutsa. Ichi ndi cholowa cha atumiki a Yehova, ndi chilungamo chao chimene chifuma kwa Ine, ati Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Samueli 22:3-4

Mulungu wa thanthwe langa, Iye ndidzamkhulupirira; chikopa changa, ndi nyanga ya chipulumutso changa, nsanja yanga yaitali, ndi populumukirapo panga; Mpulumutsi wanga, mundipulumutsa kuchiwawa. Pakuti ndi Inu ndithamangira gulu; ndi Mulungu wanga ndilumphira linga. Kunena za Mulungu, njira yake ili yangwiro; mau a Yehova anayesedwa; Iye ndiye chikopa kwa onse akukhulupirira Iye. Pakuti Mulungu ndani, koma Yehova? Ndipo thanthwe ndani, koma Mulungu wathu? Mulungu ndiye linga langa lamphamvu; ndipo Iye ayendetsa angwiro mu njira yake. Iye asandutsa mapazi ake akunga mapazi a mbawala; nandiika pa misanje yanga. Iye aphunzitsa manja anga nkhondo; kotero kuti manja anga alifula uta wamkuwa. Ndiponso munandipatsa chikopa cha chipulumutso chanu; ndi kufatsa kwanu kunandikulitsa. Munakulitsa kulunza kwanga pansi panga, ndi mapazi anga sanaterereke. Ndinapirikitsa adani anga, ndi kuwaononga; ndiponso sindinabwerere mpaka nditawatha. Ndinawatha ndi kuwapyoza, kuti sangathe kuuka, inde anagwa pansi pa mapazi anga. Ndidzaitana kwa Yehova amene ayenera timtamande; chomwecho ndidzapulumutsidwa kwa adani anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:23

Kuopa Yehova kupatsa moyo; wokhala nako adzakhala wokhuta; zoipa sizidzamgwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:7

Ndingakhale ndiyenda pakati pa nsautso, mudzandipatsa moyo; mudzatambasula dzanja lanu pa mkwiyo wa adani anu, ndipo dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:11-12

Tavalani zida zonse za Mulungu, kuti mudzakhoze kuchilimika pokana machenjerero a mdierekezi. Chifukwa kuti kulimbana kwathu sitilimbana nao mwazi ndi thupi, komatu nao maukulu, ndi maulamuliro, ndi akuchita zolimbika a dziko lapansi a mdima uno, ndi auzimu a choipa m'zakumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 2:11

Okhulupirika mauwa: Pakuti ngati tidamwalira ndi Iye, tidzakhalanso moyo ndi Iye:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:7-8

Ndidzapita kuti kuzembera mzimu wanu? Kapena ndidzathawira kuti kuzembera nkhope yanu? Ndikakwera kunka kumwamba, muli komweko; kapena ndikadziyalira ku Gehena, taonani, muli komweko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:28

Ndipo musamaopa amene akupha thupi, koma moyo sangathe kuupha; koma makamaka muope Iye, wokhoza kuononga moyo ndi thupi lomwe muGehena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:19

Musabwezere choipa, okondedwa, koma patukani pamkwiyo; pakuti kwalembedwa, Kubwezera kuli kwanga, Ine ndidzabwezera, ati Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 46:1-2

Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu m'masautso. Khalani chete, ndipo dziwani kuti Ine ndine Mulungu, Ndidzabuka mwa amitundu, ndidzabuka padziko lapansi. Yehova wa makamu ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu. Chifukwa chake sitidzachita mantha, lingakhale lisandulika dziko lapansi, angakhale mapiri asunthika, nakhala m'kati mwa nyanja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 30:5

Mau onse a Mulungu ali oyengeka; ndiye chikopa cha iwo amene amkhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 91:4

Adzakufungatira ndi nthenga zake, ndipo udzathawira kunsi kwa mapiko ake; choonadi chake ndicho chikopa chotchinjiriza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 140:4

Ndilindireni Yehova, ndisalowe m'manja mwa woipa; ndisungeni kwa munthu wachiwawa; kwa iwo akuti akankhe mapazi anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 20:1

Yehova akuvomereze tsiku la nsautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuike pamsanje;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 16:20

Ndipo Mulungu wa mtendere adzaphwanya Satana pansi pa mapazi anu tsopano lino. Chisomo cha Ambuye wathu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:19

Wolimbikira chilungamo alandira moyo; koma wolondola zoipa adzipha yekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:7

Mngelo wa Yehova azinga kuwatchinjiriza iwo akuopa Iye, nawalanditsa iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 3:3

Koma Ambuye ali wokhulupirika amene adzakukhazikitsani inu, nadzakudikirirani kuletsa woipayo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:10

Dzina la Yehova ndilo nsanja yolimba; wolungama athamangiramo napulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:18

Tidziwa kuti yense wobadwa kuchokera mwa Mulungu sachimwa, koma iye wobadwa kuchokera mwa Mulungu adzisunga yekha, ndipo woipayo samkhudza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 46:1-3

Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu m'masautso. Khalani chete, ndipo dziwani kuti Ine ndine Mulungu, Ndidzabuka mwa amitundu, ndidzabuka padziko lapansi. Yehova wa makamu ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu. Chifukwa chake sitidzachita mantha, lingakhale lisandulika dziko lapansi, angakhale mapiri asunthika, nakhala m'kati mwa nyanja. Chinkana madzi ake akokoma, nachita thovu, nagwedezeka mapiri ndi kudzala kwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:6

Kotero kuti tinena molimbika mtima, Mthandizi wanga ndiye Ambuye; sindidzaopa; adzandichitira chiyani munthu?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:6-7

Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi chiyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu. Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana chidziwitso chonse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:13

Ndipo musatitengere kokatiyesa, koma mutipulumutse kwa woipayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 41:10

usaope, pakuti Ine ndili pamodzi ndi iwe; usaopsedwe, pakuti Ine ndine Mulungu wako; ndidzakulimbitsa; inde, ndidzakuthangata; inde, ndidzakuchirikiza ndi dzanja langa lamanja la chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 23:4

Inde, ndingakhale ndiyenda m'chigwa cha mthunzi wa imfa, sindidzaopa choipa; pakuti Inu muli ndi ine; chibonga chanu ndi ndodo yanu, izi zindisangalatsa ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:31

Ndipo tidzatani ndi zinthu izi? Ngati Mulungu ali ndi ife, adzatikaniza ndani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 125:2

Monga mapiri azinga Yerusalemu, momwemo Yehova azinga anthu ake, kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 5:19

Adzakupulumutsa m'masautso asanu ndi limodzi; chinkana mwa asanu ndi awiri palibe choipa chidzakukhudza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:114

Inu ndinu pobisalapo panga, ndi chikopa changa; ndiyembekezera mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:16

Taonani, Ine ndikutumizani inu monga nkhosa pakati pa mimbulu; chifukwa chake khalani ochenjera monga njoka, ndi oona mtima monga nkhunda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 27:1

Yehova ndiye kuunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndiye mphamvu ya moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:13

amene anatilanditsa ife kuulamuliro wa mdima, natisunthitsa kutilowetsa mu ufumu wa Mwana wa chikondi chake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:8-9

Khalani odzisungira, dikirani; mdani wanu mdierekezi, monga mkango wobuma, ayendayenda ndi kufunafuna wina akamlikwire: ameneyo mumkanize okhazikika m'chikhulupiriro, podziwa kuti zowawa zomwezo zilimkukwaniridwa pa abale anu ali m'dziko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:7

Potero mverani Mulungu; koma kanizani mdierekezi, ndipo adzakuthawani inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 91:5-6

Sudzaopa choopsa cha usiku, kapena muvi wopita usana; kapena mliri woyenda mumdima, kapena chionongeko chakuthera usana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 26:3

Inu mudzasunga mtima wokhazikika mu mtendere weniweni, chifukwa ukukhulupirirani Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 91:10

palibe choipa chidzakugwera, ndipo cholanga sichidzayandikiza hema wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:21

pamwamba pa ukulu wonse, ndi ulamuliro, ndi mphamvu, ndi ufumu, ndi dzina lililonse lotchedwa, si m'nyengo ino ya pansi pano yokha, komanso mwa iyo ikudza;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 91:11

Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, akusunge m'njira zako zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:21

Musagonje kwa choipa, koma ndi chabwino gonjetsani choipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 10:4

(pakuti zida za nkhondo yathu sizili za thupi, koma zamphamvu mwa Mulungu zakupasula malinga);

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 97:10

Inu okonda Yehova, danani nacho choipa: Iye asunga moyo wa okondedwa ake; awalanditsa m'manja mwa oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 56:3-4

Tsiku lakuopa ine, ndidzakhulupirira Inu. Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ake, ndakhulupirira Mulungu, sindidzaopa; anthu adzandichitanji?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 2:7

Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni; ndiye chikopa cha oyenda molunjika;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 115:11

Inu akuopa Yehova, khulupirirani Yehova; ndiye mthandizi wao ndi chikopa chao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 1:4

amene anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu, kuti akatilanditse ife m'nyengo ya pansi pano ino yoipa, monga mwa chifuniro cha Mulungu ndi Atate wathu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 16:33

Zinthu izi ndalankhula ndi inu, kuti mwa Ine mukakhale nao mtendere. M'dziko lapansi mudzakhala nacho chivuto, koma limbikani mtima; ndalingonjetsa dziko lapansi Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 43:2

Pamene udulitsa pamadzi ndili pamodzi ndi iwe; ndi pooloka mitsinje sidzakukokolola; pakupyola pamoto sudzapsa; ngakhale lawi silidzakutentha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wachikondi, ulemerero ndi ulemu zonse kwa Inu! Lero ndikuthokozani chifukwa cha chikondi chanu ndi chifundo chanu chachikulu. Zikomo chifukwa nthawi zonse mwakhala wabwino ndi kundizungulira ndi ubwino wanu. Zikomo chifukwa pakati pa imfa munamva kulira kwanga ndi pemphero langa. Ndinu Mulungu wokhulupirika ku mawu anu. Lero nditha kunena modzidalira kuti ngakhale nditayenda m'chigwa cha mthunzi wa imfa, sindidzaopa choipa chilichonse, chifukwa Inu mudzakhala nane. Ambuye, zikomo chifukwa munandipulutsa ku imfa yauzimu ndipo tsopano mwasunga moyo wanga kundipulumutsa ku imfa yakuthupi. Zikomo chifukwa nthawi zanga zili m'manja mwanu. Lero ndikudzudzula mzimu uliwonse wa imfa womwe ukundizinga. M'dzina lamphamvu la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa