Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 91:11 - Buku Lopatulika

11 Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, akusunge m'njira zako zonse.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

11 Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, akusunge m'njira zako zonse.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

11 Chauta adzapatsa angelo ake ntchito yoti azikulonda kulikonse kumene upite.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

11 Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 91:11
11 Mawu Ofanana  

Taonani, Ine ndili pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakusunga iwe konse kumene upitako, ndipo ndidzakubwezanso iwe ku dziko lino; chifukwa kuti sindidzakusiya iwe, kufikira kuti nditachita chimene ndanena nawe.


Mngelo wa Yehova azinga kuwatchinjiriza iwo akuopa Iye, nawalanditsa iwo.


Mundikhalire thanthwe lokhalamo, lopitako kosaleka; mwalamulira kundipulumutsa; popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.


Taona, ndituma mthenga akutsogolere, kukusunga panjira, ndi kukufikitsa pamaso pomwe ndakonzeratu.


umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.


Tsoka kwa iwo amene atsikira kunka ku Ejipito kukathandizidwa, natama akavalo; nakhulupirira magaleta, pakuti ali ambiri, ndi okwera pa akavalo, pakuti ali a mphamvu zambiri; koma sayang'ana Woyera wa Israele, ngakhale kumfuna Yehova!


Tsopano uli nacho chiyani m'njira ya ku Ejipito, kumwa madzi a mtsinje wa Nailo? Uli nacho chiyani m'njira ya ku Asiriya, kumwa madzi a mtsinje wa Yufurate?


nanena naye, Ngati muli Mwana wa Mulungu, mudzigwetse nokha pansi: pakuti kwalembedwa, kuti, Adzalamula angelo ake za iwe, ndipo pa manja ao adzakunyamula iwe, ungagunde konse phazi lako pamwala.


Kodi siili yonse mizimu yotumikira, yotumidwa kuti itumikire iwo amene adzalowa chipulumutso?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa