Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


110 Mauvesi a m'Baibulo Okhudza Kuperekedwa ndi Kusakhulana

110 Mauvesi a m'Baibulo Okhudza Kuperekedwa ndi Kusakhulana

Munthu wamkulu koposa onse amene anakhalapo padziko lino lapansi anakumana ndi chinyengo chachikulu. Iye amene anali ndi mtima woyera ndi wowona mtima, wopanda choipa chilichonse, anationetsa chikondi chake ngakhale ambiri anam’tembenukira. Yesu wa ku Nazarete anachitiridwa chinyengo ndi ambiri, kuphatikizapo ineyo ndi iweyo.

Komabe, chitsanzo chake chimatiphunzitsa kuti kukhululukira ndiye mankhwala a ululu wobwera chifukwa cha chinyengo. Kumasula moyo wako ku mkwiyo ndikutsata mapazi abwino a Yesu kudzakubweretsera mphotho ya Atate.

Bisala m’chikondi cha Yesu ndi nsembe yake pa mtanda, ndipo posachedwapa udzachira ndikumwetulira chifukwa cha m’bandakucha wako watsopano. Lolani Mulungu agwire ntchito mwa inu.




Luka 22:48

Koma Yesu anati kwa iye, Yudasi, ulikupereka Mwana wa Munthu ndi chimpsompsono kodi?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:21

Ndipo mbale adzapereka mbale wake kuimfa, ndi atate mwana wake: ndipo ana adzatsutsa akuwabala, nadzawafetsa iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:56

Koma izi zonse zinachitidwa, kuti zolembedwa za aneneri zikwaniridwe. Pomwepo ophunzira onse anamsiya Iye, nathawa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:28

Munthu wokhota amautsa makani; kazitape afetsa ubwenzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 55:12-14

Pakuti si mdani amene ananditonzayo; pakadatero ndikadachilola, amene anadzikuza pa ine sindiye munthu wondida; pakadatero ndikadambisalira: Koma ameneyo ndiwe, munthu woyenerana nane, tsamwali wanga, wodziwana nane. Tinapangirana upo wokoma, tinaperekeza khamu la anthu popita kunyumba ya Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:19

Kazitape woyendayenda awanditsa zinsinsi; usadudukire woyasama milomo yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 41:9

Ngakhale bwenzi langa lenileni, amene ndamkhulupirira, ndiye amene adadyako mkate wanga, anandikwezera chidendene chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:14-16

Pomwepo mmodzi wa khumi ndi awiriwo, dzina lake Yudasi Iskariote, anamuka kwa ansembe aakulu, nati, Mufuna kundipatsa chiyani, ndipo ine ndidzampereka Iye kwa inu? Ndipo iwo anamwerengera iye ndalama zasiliva makumi atatu. Ndipo kuyambira pamenepo iye anafunafuna nthawi yabwino yakuti ampereke Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 12:6

Pakuti ngakhale abale ako, ndi nyumba ya atate wako, ngakhale iwo anakunyenga iwe; ngakhale anakufuulira iwe; usamvere iwo, ngakhale anena nawe mau abwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 24:10

Ndipo pomwepo ambiri adzakhumudwa, nadzaperekana wina ndi mnzake, nadzadana wina ndi mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:19

Kukhulupirira munthu wa chiwembu tsiku latsoka kunga dzino lothyoka ndi phazi loguluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 3:13

Koma vomereza zoipa zako, kuti walakwira Yehova Mulungu wako, ndi kupatukira mwa alendo patsinde pa mitengo yaiwisi yonse, ndipo sunamvere mau anga, ati Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zefaniya 3:4

Aneneri ake ndiwo anthu a matukutuku ndi onyenga; ansembe ao anaipsa malo opatulika, napotoza chilamulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 10:33-34

nati, Taonani, tikwera ku Yerusalemu; ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kwa ansembe aakulu ndi alembi; ndipo iwo adzamweruza kuti ayenera imfa, nadzampereka Iye kwa anthu a mitundu; ndipo adzamnyoza Iye, nadzamthira malovu, nadzamkwapula Iye, nadzamupha; ndipo pofika masiku atatu adzauka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 4:10

pakuti Dema wandisiya ine, atakonda dziko lino lapansi, napita ku Tesalonika; Kresike ku Galatiya, Tito ku Dalamatiya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 2:13

Pakuti anthu anga anachita zoipa ziwiri; anandisiya Ine kasupe wa madzi amoyo, nadziboolera zitsime, zitsime zong'aluka, zosakhalamo madzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 49:3-4

Rubeni, ndiwe woyamba wanga, mphamvu yanga ndi chiyambi cha mphamvu yanga; ulemu wopambana, ndi mphamvu yopambana. m'phanga lili m'munda wa Makipela, umene uli patsogolo pa Mamure, m'dziko la Kanani, limene Abrahamu analigula kwa Efuroni Muhiti pamodzi ndi munda, likhale poikira pake: pamenepo anaika Abrahamu ndi Sara mkazi wake; pamenepo anaika Isaki ndi Rebeka mkazi wake: pamenepo ndinaika Leya: munda ndi phanga lili m'menemo, zinagulidwa kwa ana a Hiti Pamene Yakobo anatha kulangiza ana ake aamuna, anafunya mapazi ake pakama, natsirizika, nasonkhanitsidwa kwa anthu a mtundu wake. Wobwabwada ngati madzi; sudzapambana; chifukwa unakwera pa kama wa atate wako; pamenepo unaipitsapo; anakwera paja ndigonapo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Samueli 13:28-29

Ndipo Abisalomu analamulira anyamata ake, nati, Inu mukhale maso, mtima wa Aminoni ukasekera ndi vinyo, ndipo ine ndikati kwa inu, Kanthani Aminoni; pamenepo mumuphe, musaope; sindine ndakulamulirani inu mulimbike, chitani chamuna. Ndipo anyamata a Abisalomu anamchitira Aminoni monga umo Abisalomu anawalamulira. Pomwepo ana aamuna onse a mfumu ananyamuka, nakwera munthu yense pa nyuru yake, nathawa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 55:20-21

Anatulutsa manja ake awagwire iwo akuyanjana naye, anaipsa pangano lake. Pakamwa pake mposalala ngati mafuta amkaka, koma mumtima mwake munali nkhondo, mau ake ngofewa ngati mafuta oyenga, koma anali malupanga osololasolola.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:4

Simoni Mkanani, ndi Yudasi Iskariote amenenso anampereka Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 16:17-18

Ndipo ndikudandaulirani, abale, yang'anirani iwo akuchita zopatutsana ndi zophunthwitsa, kosalingana ndi chiphunzitsocho munachiphunzira inu; ndipo potolokani pa iwo. Pakuti otere satumikira Ambuye wathu Khristu, koma mimba yao; ndipo ndi mau osalaza ndi osyasyalika asocheretsa mitima ya osalakwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 109:5-8

Ndipo anandisenza choipa m'malo mwa chokoma, ndi udani m'malo mwa chikondi changa. Muike munthu woipa akhale mkulu wake; ndi mdani aime padzanja lamanja lake. Ponenedwa mlandu wake atuluke wotsutsika; ndi pemphero lake likhale ngati kuchimwa. Masiku ake akhale owerengeka; wina alandire udindo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:33

Musanyengedwe; mayanjano oipa aipsa makhalidwe okoma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:5

Mboni yokhulupirika siidzanama; koma mboni yonyenga imalankhula zonama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 33:1

Tsoka kwa iwe amene usakaza, chinkana sunasakazidwe; nupangira chiwembu, chinkana sanakupangire iwe chiwembu! Utatha kusakaza, iwe udzasakazidwa; ndipo utatha kupangira chiwembu, iwo adzakupangira iwe chiwembu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 31:11

Ndakhala chotonza chifukwa cha akundisautsa onse, inde, koposa kwa anansi anga; ndipo anzanga andiyesa choopsa; iwo akundipenya pabwalo anandithawa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:7

Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti chimene munthu achifesa, chimenenso adzachituta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:23

tigwiritse chivomerezo chosagwedera cha chiyembekezo chathu, pakuti wolonjezayo ali wokhulupirika;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:6

Kulasa kwa bwenzi kuli kokhulupirika; koma mdani apsompsona kawirikawiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 3:1-5

Koma zindikira ichi, kuti masiku otsiriza zidzafika nthawi zowawitsa. Koma iwe watsatatsata chiphunzitso changa, mayendedwe, chitsimikizo mtima, chikhulupiriro, kuleza mtima, chikondi, chipiriro, mazunzo, kumva zowawa; zotere zonga anandichitira mu Antiokeya, mu Ikonio, mu Listara, mazunzo otere onga ndawamva; ndipo m'zonsezi Ambuye anandilanditsa. Ndipo onse akufuna kukhala opembedza m'moyo mwa Khristu Yesu, adzamva mazunzo. Koma anthu oipa ndi onyenga, adzaipa chiipire, kusokeretsa ndi kusokeretsedwa. Koma ukhalebe iwe mu izi zimene waziphunzira, nutsimikizika mtima nazo, podziwa amene adakuphunzitsa; ndi kuti kuyambira ukhanda wako wadziwa malembo opatulika, okhoza kukupatsa nzeru kufikira chipulumutso, mwa chikhulupiriro cha mwa Khristu Yesu. Lemba lililonse adaliuzira Mulungu, ndipo lipindulitsa pa chiphunzitso, chitsutsano, chikonzero, chilangizo cha m'chilungamo: kuti munthu wa Mulungu akhale woyenera, wokonzeka kuchita ntchito iliyonse yabwino. Pakuti anthu adzakhala odzikonda okha, okonda ndalama, odzitamandira, odzikuza, amwano, osamvera akuwabala, osayamika, osayera mtima, opanda chikondi chachibadwidwe, osayanjanitsika, akudierekeza, osakhoza kudziletsa, aukali, osakonda abwino, achiwembu, aliuma olimbirira, otukumuka mtima, okonda zokondweretsa munthu, osati okonda Mulungu; akukhala nao maonekedwe a chipembedzo, koma mphamvu yake adaikana; kwa iwonso udzipatule.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 12:1-2

Pulumutsani, Yehova; pakuti wofatsa wasowa; pakuti okhulupirika achepa mwa ana a anthu. Amanena za bodza munthu yense ndi mnansi wake, amanena ndi mlomo wothyasika, ndi mitima iwiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 4:10

Pakuti akagwa, wina adzautsa mnzake; koma tsoka wakugwa wopanda womnyamutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 17:13-14

Ukani Yehova, Mumtsekereze, mumgwetse, landitsani moyo wanga kwa woipa ndi lupanga lanu; kwa anthu, ndi dzanja lanu, Yehova, kwa anthu a dziko lapansi pano amene cholowa chao chili m'moyo uno, ndipo mimba yao muidzaza ndi chuma chanu chobisika; akhuta mtima ndi ana, nasiyira ana amakanda zochuluka zao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 9:4

Muchenjere naye yense mnansi wake, musakhulupirire yense mbale wake; pakuti abale onse amanyenga, ndipo anansi onse adzayenda ndi maugogodi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Hoseya 6:7

Koma iwo analakwira chipangano ngati Adamu, m'mene anandichitira monyenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:158

Ndinapenya ochita monyenga, ndipo ndinanyansidwa nao; popeza sasamalira mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 18:30

Chifukwa chake ndidzakuweruzani inu, nyumba ya Israele, yense monga mwa njira zake, ati Ambuye Yehova. Bwererani, nimutembenukire kuleka zolakwa zanu zonse, ndipo simudzakhumudwa nazo, ndi kuonongeka nayo mphulupulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:31-32

Pamenepo Yesu ananena kwa iwo, Inu nonse mudzakhumudwa chifukwa cha Ine usiku uno; pakuti kwalembedwa, Ndidzakantha mbusa, ndipo zidzabalalika nkhosa za gulu. Koma nditauka ndidzatsogolera inu ku Galileya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 3:1

Yehova! Ha! Achuluka nanga akundisautsa ine! Akundiukira ine ndi ambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 12:52-53

pakuti kuyambira tsopano adzakhala m'nyumba imodzi anthu asanu, atatu adzatsutsana ndi awiri, ndi awiri adzatsutsana ndi atatu. Adzatsutsana atate ndi mwana wake, ndi mwana ndi atate wake; amake adzatsutsana ndi mwana wamkazi, ndi mwana wamkazi ndi amake, mpongozi adzatsutsana ndi mkazi wa mwana wake, ndi mkaziyo ndi mpongozi wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:11-13

Koma pamene Kefa anadza ku Antiokeya ndinatsutsana naye pamaso pake, pakuti anatsutsika wolakwa. Pakuti asanafike ena ochokera kwa Yakobo, anadya pamodzi ndi amitundu; koma atadza iwo, anadzibweza, ndi kudzipatula yekha, pakuopa iwo a ku mdulidwe. Ndipo Ayuda otsala anawagwiranso m'maso pamodzi naye; kotero kuti Barnabasinso anatengedwa ndi kugwira m'maso kwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:5

Wosyasyalika mnzake atcherera mapazi ake ukonde.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 55:6-8

Ndipo ndinati, Ha, wina akadandipatsa mapiko onga a njiwa! Mwenzi nditauluka, ndi kukhaliratu. Onani, ndikadathawira kutali, ndikadagona m'chipululu. Ndikadafulumira ndipulumuke kumphepo yolimba ndi namondwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 5:26-28

Pakuti mwa anthu anga aoneka anthu oipa; adikira monga akutcha misampha; atcha khwekhwe, agwira anthu. Monga chikwere chodzala ndi mbalame, chomwecho nyumba zao zadzala ndi chinyengo; chifukwa chake akula, alemera. Anenepa, anyezimira; inde apitiriza kuchita zoipa; sanenera ana amasiye mlandu wao, kuti apindule; mlandu wa aumphawi saweruza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:1

Momwemo pakutaya choipa chonse, ndi chinyengo chonse, ndi maonekedwe onyenga, ndi kaduka, ndi masinjiriro onse,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 26:4-5

Sindinakhala pansi ndi anthu achabe; kapena kutsagana nao anthu othyasika. Ndidana nao msonkhano wa ochimwa, ndipo sindidzakhala nao pansi ochita zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 24:12

Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa kusaweruzika, chikondano cha anthu aunyinji chidzazilala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:10

Pakuti muzu wa zoipa zonse ndiwo chikondi cha pa ndalama; chimene ena pochikhumba, anasochera, nataya chikhulupiriro, nadzipyoza ndi zowawa zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 1:21

Mzinda wokhulupirika wasanduka wadama! Wodzala chiweruzowo! Chilungamo chinakhalamo koma tsopano ambanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 10:1

Ntchentche zakufa zinunkhitsa moipa ndipo zioletsa mafuta onunkhira a sing'anga; chomwecho kupusa kwapang'ono kuipitsa iye amene atchuka chifukwa cha nzeru ndi ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:150

Otsata zachiwembu andiyandikira; akhala kutali ndi chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:6

Anthu ambiri abukitsa yense kukoma mtima kwake; koma ndani angapeze munthu wokhulupirika?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 144:8

amene pakamwa pao alankhula zachabe, ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lachinyengo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 33:31

Ndipo akudzera monga amadzera anthu, nakhala pansi pamaso pako ngati anthu anga, namva mau ako, koma osawachita; pakuti pakamwa pao anena mwachikondi, koma mtima wao utsata phindu lao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:9

Wobisa cholakwa afunitsa chikondano; koma wobwerezabwereza mau afetsa ubwenzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:12

Chifukwa chake iye wakuyesa kuti ali chilili, ayang'anire kuti angagwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 55:23

Koma Inu, Mulungu, mudzawatsitsira kudzenje la chionongeko. Anthu okhetsa mwazi ndi achinyengo masiku ao sadzafikira nusu; koma ine ndidzakhulupirira Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:15

Yang'anirani mupewe aneneri onyenga, amene adza kwa inu ndi zovala zankhosa, koma m'kati mwao ali mimbulu yolusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:38-39

Pakuti ndakopeka mtima kuti ngakhale imfa, ngakhale moyo, ngakhale angelo, ngakhale maufumu, ngakhale zinthu zilipo, ngakhale zinthu zilinkudza, ngakhale zimphamvu, ngakhale utali, ngakhale kuya, ngakhale cholengedwa china chilichonse, sichingadzakhoze kutisiyanitsa ife ndi chikondi cha Mulungu, chimene chili mwa Khristu Yesu Ambuye wathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 3:12

Tapenyani, abale, kuti kapena ukakhale mwa wina wa inu mtima woipa wosakhulupirira, wakulekana ndi Mulungu wamoyo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:113

Ndidana nao a mitima iwiri; koma ndikonda chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:15

Koma ngati mulumana ndi kudyana, chenjerani mungaonongane.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 27:10

Pakuti wandisiya atate wanga ndi amai wanga, koma Yehova anditola.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:20

Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru: koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 59:14-15

Ndipo chiweruziro chabwerera m'mbuyo, ndi chilungamo chaima patali; pakuti choona chagwa m'khwalala, ndi kuongoka sikungalowe. Inde choona chisoweka; iye amene asiya choipa, zifunkhidwa zake; ndipo Yehova anaona ichi, ndipo chidamuipira kuti palibe chiweruzo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:8

Khalani odzisungira, dikirani; mdani wanu mdierekezi, monga mkango wobuma, ayendayenda ndi kufunafuna wina akamlikwire:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:28

Pakuti Yehova akonda chiweruzo, ndipo sataya okondedwa ake. Asungika kosatha, koma adzadula mbumba za oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 6:13-14

Pakuti kuyambira wamng'ono kufikira wamkulu onse akhala akusirira; ndiponso kuyambira mneneri kufikira wansembe onse achita monyenga. Ndiponso apoletsa bala la anthu anga pang'onong'ono, ndi kuti, Mtendere, mtendere; koma palibe mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 24:10-13

Ndipo pomwepo ambiri adzakhumudwa, nadzaperekana wina ndi mnzake, nadzadana wina ndi mnzake. Ndipo aneneri onama ambiri adzauka, nadzasokeretsa anthu ambiri. Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa kusaweruzika, chikondano cha anthu aunyinji chidzazilala. Koma iye wakulimbika chilimbikire kufikira kuchimaliziro, yemweyo adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:5

Mboni yonama sidzakhala yosalangidwa; wolankhula mabodza sadzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 62:4

Komatu amkhalira upo kuti amkankhire pansi ulemu wake; akondwera nao mabodza; adalitsa ndi m'kamwa mwao, koma atemberera mumtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:47-48

Pamene Iye anali chilankhulire, taonani, khamu la anthu, ndipo iye wotchedwa Yudasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anawatsogolera; nayandikira Yesu kumpsompsona Iye. Koma Yesu anati kwa iye, Yudasi, ulikupereka Mwana wa Munthu ndi chimpsompsono kodi?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:30

akazitape, osinjirira, akumuda Mulungu, achipongwe, odzitama, amatukutuku, oyamba zoipa, osamvera akulu ao,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:26-27

Pakuti tikachimwa ife eni ake, titatha kulandira chidziwitso cha choonadi, siitsalanso nsembe ya kwa machimo, koma kulindira kwina koopsa kwa chiweruziro, ndi kutentha kwake kwa moto wakuononga otsutsana nao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 3:1

Kanthu kalikonse kali ndi nthawi yake ndi chofuna chilichonse cha pansi pa thambo chili ndi mphindi yake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 15:4

M'maso mwake munthu woonongeka anyozeka; koma awachitira ulemu akuopa Yehova. Atalumbira kwa tsoka lake, sasintha ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:1

Abale, ngatinso munthu agwidwa nako kulakwa kwakuti, inu auzimu, mubweze wotereyo mu mzimu wa chifatso; ndi kudzipenyerera wekha, ungayesedwe nawenso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 109:3

Ndipo anandizinga ndi mau a udani, nalimbana nane kopanda chifukwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 50:6

Ndinapereka msana wanga kwa omenya, ndi masaya anga kwa iwo amene anakudzula tsitsi langa; sindinabisire nkhope yanga manyazi ndi kulavulidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:9

Chikondano chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choipa; gwirizana nacho chabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 26:24-26

Wakuda mnzake amanyenga ndi milomo yake; koma akundika chinyengo m'kati mwake. Pamene akometsa mau ake usamkhulupirire; pakuti m'mtima mwake muli zonyansa zisanu ndi ziwiri. Angakhale abisa udani wake pochenjera, koma udyo wake udzavumbulutsidwa posonkhana anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 101:5

Wakuneneza mnzake m'tseri ndidzamdula; wa maso odzikuza ndi mtima wodzitama sindidzamlola.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:25

Ndipo Yudasi, womperekayo anayankha nati, Kodi ndine, Rabi? Iye ananena kwa iye, Iwe watero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:17

Bwenzi limakonda nthawi zonse; ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 18:30-32

Chifukwa chake ndidzakuweruzani inu, nyumba ya Israele, yense monga mwa njira zake, ati Ambuye Yehova. Bwererani, nimutembenukire kuleka zolakwa zanu zonse, ndipo simudzakhumudwa nazo, ndi kuonongeka nayo mphulupulu. Tayani, ndi kudzichotsera zolakwa zanu zonse zimene munalakwa nazo, ndi kudzifunira mtima watsopano, ndi mzimu watsopano; pakuti mudzaferanji inu, nyumba ya Israele? Pakuti sindikondwera nayo imfa ya wakufayo, ati Ambuye Yehova; chifukwa chake bwererani, nimukhale ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:20

Kodi uyenera kuyanjana ndi Inu mpando wachifumu wa kusakaza, wakupanga chovuta chikhale lamulo?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 6:4-6

Pakuti sikutheka kuwakonzanso, atembenuke mtima, iwo amene anaunikidwa pa nthawi yake, nalawa mphatso ya Kumwamba, nakhala olandirana naye Mzimu Woyera, nalawa mau okoma a Mulungu, ndi mphamvu ya nthawi ilinkudza, koma anagwa m'chisokero; popeza adzipachikiranso okha Mwana wa Mulungu, namchititsa manyazi poyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:8-9

Kuthawira kwa Yehova nkokoma koposa kukhulupirira munthu. Kuthawira kwa Yehova nkokoma koposa kukhulupirira akulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 54:17

Palibe chida chosulidwira iwe chidzapindula; ndipo lilime lonse limene lidzakangana nawe m'chiweruzo udzalitsutsa. Ichi ndi cholowa cha atumiki a Yehova, ndi chilungamo chao chimene chifuma kwa Ine, ati Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:13

Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi; koma wokhulupirika mtima abisa mau.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:4

ndicho chifukwa cha abale onyenga olowezedwa m'tseri, amene analowa m'tseri kudzazonda ufulu wathu umene tili nao mwa Khristu Yesu, kuti akatichititse ukapolo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 41:5-6

Adani anga andinenera choipa, ndi kuti, adzafa liti, ndi kutayika dzina lake? Ndipo akadza kundiona wina angonena bodza; mumtima mwake adzisonkhera zopanda pake, akanka nayenda namakanena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 12:4-5

Ndipo ndinena kwa inu, abwenzi anga, Musaope iwo akupha thupi, ndipo akatha ichi alibe kanthu kena angathe kuchita. Khalani okonzeka inunso; chifukwa nthawi imene simulingirira, Mwana wa Munthu akudza. Ndipo Petro anati, Ambuye, kodi fanizo ili mwalinena kwa ife, kapena kwa onse? Ndipo Ambuye anati, Ndani tsono ali mdindo wokhulupirika ndi wanzeru, amene mbuye wake adzamuika kapitao wa pa banja lake, kuwapatsa iwo phoso lao pa nthawi yake? Wodala kapoloyo amene mbuye wake pakufika, adzampeza alikuchita chotero. Ndinena ndinu zoona, kuti adzamuika iye kapitao wa pa zonse ali nazo. Koma kapolo uyo akanena mumtima mwake, Mbuye wanga azengereza kudza; ndimo akayamba kupanda anyamata ndi adzakazi ndi kudya ndi kumwa, ndi kuledzera; mbuye wa kapolo uyo adzafika tsiku lakuti samuyembekezera, ndi nthawi yakuti saidziwa, nadzamdula iye pakati nadzamuika dera lake pamodzi ndi anthu osakhulupirira. Ndipo kapolo uyo, wodziwa chifuniro cha mbuye wake, ndipo sanakonze, ndi kusachita zonga za chifuniro chakecho, adzakwapulidwa mikwapulo yambiri. Koma iye amene sanachidziwe, ndipo anazichita zoyenera mikwapulo, adzakwapulidwa pang'ono. Ndipo kwa munthu aliyense adampatsa zambiri, kwa iye adzafuna zambiri; ndipo amene anamuikizira zambiri, adzamuuza abwezere zoposa. Ine ndinadzera kuponya moto padziko lapansi; ndipo ndifunanji ngati unatha kuyatsidwa? Koma ndidzakulangizani amene muzimuopa; taopani Iye amene atatha kupha ali ndi mphamvu yakutaya ku Gehena, inde, ndinena ndinu opani ameneyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:37

Koma manenedwe anu akhale, Inde, inde; Iai, iai; ndipo choonjezedwa pa izo chichokera kwa woipayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:6

Kupata chuma ndi lilime lonama ndiko nkhungu yoyendayenda, ngakhale misampha ya imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:3-4

Pakuti ndinachitira nsanje odzitamandira, pakuona mtendere wa oipa. Pakuti palibe zomangira pakufa iwo, ndi mphamvu yao njolimba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 4:1-2

Koma Mzimu anena monenetsa, kuti m'masiku otsiriza ena adzataya chikhulupiriro, ndi kusamala mizimu yosocheretsa ndi maphunziro a ziwanda, Pakuti kukalingako tigwiritsa ntchito ndi kuyesetsa, chifukwa chiyembekezo chathu tili nacho pa Mulungu wamoyo, amene ali Mpulumutsi wa anthu onse, makamaka wa okhulupirira. Lamulira izi, nuziphunzitse. Munthu asapeputse ubwana wako; komatu khala chitsanzo kwa iwo okhulupirira, m'mau, m'mayendedwe, m'chikondi, m'chikhulupiriro, m'kuyera mtima. Kufikira ndidza ine, usamalire kuwerenga, kuchenjeza, kulangiza. Usanyalapse mphatsoyo ili mwa iwe, yopatsidwa kwa iwe mwa chinenero, pamodzi ndi kuika kwa manja a akulu. Izi uzisamalitse; mu izi ukhale; kuti kukula mtima kwako kuonekere kwa onse. Udzipenyerere wekha, ndi chiphunzitsocho. Uzikhala mu izi; pakuti pochita ichi udzadzipulumutsa iwe wekha ndi iwo akumva iwe. m'maonekedwe onyenga a iwo onena mabodza, olochedwa m'chikumbu mtima mwao monga ndi chitsulo chamoto;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:20

Pakuti kulibe wolungama pansi pano amene achita zabwino osachimwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:32

Wokana mwambo apeputsa moyo wake; koma wosamalira chidzudzulo amatenga nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:36

ndipo apabanja ake a munthu adzakhala adani ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:21-23

Asonkhana pamodzi pa moyo wa wolungama, namtsutsa wa mwazi wosachimwa. Koma Yehova wakhala msanje wanga; ndi Mulungu wanga thanthwe lothawirapo ine. Ndipo anawabwezera zopanda pake zao, nadzawaononga m'choipa chao; Yehova Mulungu wathu adzawaononga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:4

Msatero ai. Koma Mulungu akhale woona, ndipo anthu onse akhale onama; monga kwalembedwa, Kuti Inu mukayesedwe wolungama m'maneno anu, ndi kuti mukapambane m'mene muweruzidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:12

Pakuti mau a Mulungu ali amoyo, ndi ochitachita, ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse, napyoza kufikira kugawira moyo ndi mzimu, ndi zimfundo ndi mafuta a m'mafupa, nazindikiritsa zolingirira ndi zitsimikizo za mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:20-21

kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko, njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 59:2

koma zoipa zanu zakulekanitsani inu ndi Mulungu wanu; ndipo machimo anu abisa nkhope yake kwa inu, kuti Iye sakumva.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 54:5

Adzabwezera choipa adani anga, aduleni m'choonadi chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 6:16-19

Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi Yehova azida; ngakhale zisanu ndi ziwiri zimnyansa: Maso akunyada, lilime lonama, ndi manja akupha anthu osachimwa; mtima woganizira ziwembu zoipa, mapazi akuthamangira mphulupulu m'mangum'mangu; mboni yonama yonong'ona mabodza, ndi wopikisanitsa abale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye, ndikukutamandani chifukwa ndinu Wolungama, Woyera, Woyenera kutamandidwa ndi kupembedzedwa konse. Ndinu Mulungu wanga, mtendere wanga pakati pa mkuntho, ndi thandizo langa lapafupi. Ambuye, m'dzina la Yesu, ndikubwera kwa inu pakati pa chisoni ichi chomwe ndikukumana nacho monga chipongwe. Ndithandizeni kukhululukira chifukwa ndikumva kuti mphamvu zanga zatha, koma ndikumvetsa kuti pano mphamvu zanu ziyamba kugwira ntchito. Atate, choyamba chiritsani maganizo anga ndi mtima wanga, musalole kuti mkwiyo ndi chisoni chomwe ndikumva chiwononge moyo wanga, kapena ubale womwe ndili nawo ndi inu. Zoonadi, kukhulupirika kwanu ndi chikondi chanu ndizosayerekezeka Mulungu, chikondi chenicheni chimachokera kwa inu ndipo kudzera mwa Mzimu Woyera wanu, chifukwa chake ndikupemphani mundidzaze ndi chikondi kwa munthu uyu yemwe ndi zochita ndi mawu ake anayesa kuwononga mtima wanga, muchitire chifundo, chifukwa mawu anu amati: «Ambiri adzakhumudwa, ndipo adzaperekedzana, ndipo adzadana.»  Dalitsani Ambuye, chifukwa mawu anu akhala pothawirapo panga ndipo chikondi chanu chilipo pamene ndikudutsa m’chipongwe ichi. Inu Yesu munaperekedwa, munayesedwa, munakanidwa, munanyozedwa ndi kunyozedwa chifukwa cha ine, kuti mulipire mtengo wa zoipa zanga, pa inu Ambuye munali mtendere wanga. Ndipangitseni kumvetsa kuti anthufe ndife ofooka ndi osasinthasintha, ndipo timakonda kulakwitsa kapena kuti ena atilakwitse. Yeretsani maganizo anga, mtima wanga ndi malingaliro omwe mdani anayesa kubzala mwa ine awachotse m'dzina la Yesu. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa